Category Archives: Uncategorized

22-1231 Mpikisano

Uthenga: 62-1231 Mpikisano

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Nkhosa Zam’dera,

Ndikufuna kudzakhalanso ndi Mgonero m’manyumba zathu pa Madzulo a Chaka Chatsopano, pa 31 December. Malangizo momwe mungapezere waini, ndi kuphika mkate wa Mgonero angapezeke m’malinki ali pansi. Linki yomunga daunilode wamawu amtunduwu upezeka posachedwa patsamba lathu. Kapena, munga lize mawu omvera kuchokera pa pulogalamu ya Lifeline.

Kwa anthu akudera la Jeffersonville, munga teng wainivi wa Mgonero pachisanu, Disembala 30, pakati pa 1:00 – 4:00 pm, pansi pa denga la VGR.

Timvera 62-1231 ku Shoshana, kuyambira 5:00 pm EST pa satade, Disembala 31st. M’bale Branham akadzabweretsa Uthenga wa Madzulo wa Chaka Chatsopano, tidzaimilika tepu ndikukhala ndi pafupifupi mphindi 10 za Nyimbo za Kulambira pamene tikukonzekera Mgonero wa Ambuye. tidzayamba anso tepi pamalo pomwe M’bale Branham ayambila utumiki wa Mgonero. Pa tepi iyi, iye wasiya kusambika mapazi gawo la utumiki, chimene ife tizachita.

Pamene tikutembenukira ku chaka china mu Utumiki Wake, tiyeni tiperekenso mwewo yathu kwa Iye mwatsopano kupitira mu kumva Mawu poyamba, ndiye kudya nawo Mgonero Wake. Ndi mwayi wamtengo wapatali bwanji umene tili nawo wokonza nyumba zathu kukhala Malo Opatulika kuti tilandire Mfumu ya Mafumu kuti ibwere kudzatigwirizanitsa ise.

Mulungu akudalitseni,

M’bale Joseph

22-1225 Kuchita Manyazi

Uthenga: 65-0711 Kuchita Manyazi

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mkwati Rebekah,

Atate anatumiza mtumiki wake wokhulupirika, Eliezere, kukasanka Mkwati Wake Rebeka. Ife tamuziba iye, mtumiki Wake wa mngelo wachisanu ndi chiwiri, William Marrion Branham, yemwe Iye anamutuma kuti: Amuyitane, Asonkhanitse, Atsogolere ndipo potsiriza Atidziwitse ife, kwa Iye.

Iye watipatsa ife kutsanulidwa kwakukulu kwa Mphamvu Yake Yofulumizitsa ndipo watifikitsa ife kuziba udindo wathu, malo athu, ndi maudindo athu, pokhala anthu oitanidwa, olekanitsidwa ndi dziko, odzipereka kwa Mulungu. Iye akutitsogolera ndi kutitsogolera mu zinthu zomwe timachita ndi kunena, kubweretsa ulemu ndi ulemerero ku Dzina Lake.

Palibe kanthu, paliponse, kangatilekanitse ife kwa Izo, PALIBE. Ndife otetezedwa Kwamuyayaya mu Ufumu wa Mulungu. Atate watidinda Chidindo Chake ife mpaka kumapeto kwa kopita kwathu.

Satana amatikhonya ISE kuseni ndi usiku. Iye amanena chirichonse kwa ife, ndipo amatitsutsa ife, ndipo amayesa kutipangitsa ife kuganiza kuti ife sitiri Mkwati ameneyo. Amaponya chilichonse m’njira yathu kuyesa kutisokoneza, monga matenda ndi mavuto, koma sitimumvera. Mphamvu yofulumizitsa iyo ili TSOPANO mwa ife ndipo ife tasindikizidwa ndi kukhazikika pa Mawu amenewo. Tikutoloka pa kamelo yathu, kuthamangira kwa Iye popita ku Mgonero wathu waukulu wa Ukwati.

Sitichita manyazi ndi zomwe timakhulupirira; m’malo mwake, ife tikufuna kuti dziko lidziwe, IFE NDIFE ANTHU AMATEPI AMENE AMAKHULUPIRIRA MAWU ONSE OLANKHULIDWA NDI MNENERI WAKE WOKHULUPIRIKA WA ELIEZA yemwe Iye anamutuma kuti akamuitane ndi kutsogolera MKWATI WAKE WA REBEKA. Ife sitimawonjezeranso kapena kuchotsa Mawu AMODZI. Uthenga uwu ndi Mtheradi wathu.

Angakhoze bwanji munthu yemwe ali wodzazidwa ndi Mzimu Woyera, wodzaza ndi Mphamvu ya Mulungu, ndi chikondi cha Mulungu mu mtima mwake, kulankhula kwa munthu maminiti pang’ono chabe ndi kusakamba chinachake cha Uthenga umene iye wangowumva kumene pa Tepi?

Mukakumana ndi anthu amene amadzinenera kuti ndi okhulupirira mu Uthenga wa nthawi yotsiriza ino, mukhoza kuyankhula nawo maminiti pang’ono chabe ndipo mukhoza kudziwa kumene iwo akuyima pa kuliza matepi. Iwo mwina ndi Anthu a Tepi kapena ayi.

Ndi shosaganizila kuti amaona kuti ndi chamanyazi, kapenanso cholakwika, ngati munganene kuti mumaliza matepi kutchalitchi kwanu kapena kunyumba. Iwo amamverera kuti ndi zotsutsana ndi Mawu ndipo osati Njira yoperekedwa ndi Mulungu. Mumaonesedwa pansi chifukwa mumati ndinu “Munthu Watepi”.
[12/24, 12:38 PM] Br moya: Atumiki omwe amaliza matepi m’mipingo yawo amatsutsidwa, ndipo amaitanidwa aulesi. Ndipo ngati inu mumvetsera kwa tepi yomweyo pa nthawi yomweyo, chabwino, sindinu nkomwe mtumiki, ndinu chipembedzo, kapena wopempela munthu.

Ine ndikuganiza anthu onse aja omwe anachita conekiti pa telefoni mu mipingo ndi nyumba zawo, akumvetsera kwa M’bale Branham onse pa nthawi imodzi, iwo ayenera kuti anali achipembedzo nawonso. Ayenera kuti sianali mu pulogalamu la Mulungu. Sanachite manyazi NDIPO NAIFE.

Patawi chabe zochepa mukalankhula ndi anthu, amakudziwitsani pomwepo pomwe ayima: Inde, timadinikiza kuliza. Inde, timamvetsera matepi Lamlungu mu Mpingo kapena nyumba zathu. Inde, tepi yomweyo, na nthawi yomweyo.

Chifukwa chiyani ena amati, “Timapita kutchalitchi Lamlungu m’mawa, Lamlungu usiku, ndi Lachitatu usiku. Tili ndi abusa abwino; Iye amazifotokoza momveka bwino komanso momveka bwino kuti ife timvetse. Iye akufotokoza Uthenga kuti ine ndiwumvetse Iwo. Inu muyenera kukhala ndi utumiki kuti mukhale Mkwati. M’bale Branham sananene kuti mukaziliza matepi mu mpingo.”

Munena chiyani ndiye chofunikira kwambiri? Zomwe alaliki amanena, zomwe M’bale Joseph akunena, kapena zomwe Liwu lomwe la Mulungu likunena pa Tepi? Mtheradi wanu ndi chiyani? Kodi pa Tepi pali chiyani, kapena zomwe wina akunena?

Utumiki ndi wabwino, ndipo mu Mawu. Timawafuna. Koma CHOFUNIKA KWAMBIRI ndi chiyani, kulalikira kapena Matepi?

Ngati Matepi sali chinthu chofunikira kwambiri mu moyo wanu waumuntu, mu moyo wa mpingo wanu, ndiye chinachake chalakwika. Inu mwachoka pa Chifuniro Chabwino cha Mulungu. BWELANI MU NJILA.

Pamene munthu akomana konse ndi Mulungu; osati mu ntchito zina zokhudza maganizo, ziphunzitso za chipembedzo cikhulupililo kapena ciphunziso zozilimbikitsa, koma akafika pa malo monga mmene Mose anacitila. Kumbuyo kwadesati, kuyenda maso ndi maso ndi Mulungu Wamphamvuzonse, ndipo iwe umawona Liwu likulankhula kwa iwe, kosapusana ndi Mawu ndi lonjezo la ntawi, pali chinachake chikuchita kwa iwe! Mwaona, inu simukuchita nawo manyazi Iwo, Iwo amachita chinachake kwa inu.

Masiku atu, chofimba chachikhalidwe chimenecho chang’ambika. Apa payima Lawi la Moto, likuwonetsera Mawu a tsiku lino. Umulungu aphimbidwa mu thupi la munthu. Ulemerero wa Shekinah wa lero. Mulungu ayima ndi kuyankhula pamaso pathu, aphimbidwa mu thupi la munthu.

Mose anali nawo Mawu. Tsopano kumbukirani, Mawu ana wonetseredwa, Mose anali Mose kachiwiri. Mwaona? Koma pamene Mawu amenewo anali mwa iye kuti aperekedwe, iye anali Mulungu; chabwino, iye sanali Mose panonso. Iye anali nawo Mawu a Ambuye a m’badwo umenewo.

Khrisimasi yomwe ife a Rebeka tidzakhala nayo Lamlungu lino. Tsiku lonse, nthawi zosiyanasiyana tsiku lonse. Tidzamva Eliezere wathu akuitana Mkwati wake ndipo tidzakhala tikumuuza kuti sitikuchita manyazi.

Ambuye akupatseni inu Khrisimasi yabwino, yodzazidwa ndi “KUKHALA KWAKE”.

Bro. Joseph Branham

Uthenga: 65-0711 Manyazi

Lemba: Marko 8:34-38

Ndandanda ya Khrisimasi

Okondedwa Abale ndi Alongo,

Chifukwa cha Khrisimasi ili pa mulugu chaka chino, ndamva mumtima mwanga kuti tisakhale ndi nthawi yoti timve Uthenga tsiku limenelo. Mabanja ambiri ali ndi ana ang’ono omwe amasangala kutsegula mphatso zawo m’mawa wa Khrisimasi, ndipo zingakhale zovuta kwa iwo kukhazikika kuti amve Uthenga kapena kuwapangitsa kuti ayembekeze mpaka nthawi ina.

Ndipo, komachabe, pa Khrisimasi, mukudziwa, ana aang’ono, sungawauze mosiyana. Iwo, basi, ndi nthawi ya Khrisimasi kwa iwo. Ndipo iwo siangankale apachikidwe masokosi awo aang’ono, pagankala chinachake. Ndi mwambo, ngakhale mu ziko lathu, kuti iwo amapachika sokosi, ndi chinachake chimzake. Bwanji, ine ndinatero, pamene ine ndinali mwana, ndipo—ndipo ngakhale monga—kutalika kwa Lemba, njira yopunthidwa monga iyo iliri. Koma, ana amamva ana ena akunena kuti, “Chabwino, ndalandira izi pa Khrisimasi. Ndapeza izi.” Ana aang’ono amaima pozungulira, langanani, inu mukudziwa. Inu, inu simungakhoze kuwapangitsa iwo kumvetsa. Mwaona? Chifukwa chake, Khrisimasi inabwela kunkala. Inde.

Pangakale ena omwe angakonde kuwuka kuseniseni ndikumva Uthenga, popeza ali ndi mapulani ndi achibale awo tsiku lomwelo. Choncho ndasankha kuti banja lililonse lisankhe nthawi yomwe ingagwirizane ndi nbanja yawo yomvera Uthenga. Tidzaulutsa Uthenga pa Lifeline katatu kosiyana pa Tsiku la Khrisimasi: 9:00 A.M. – 12:00 PM. – 5:00 P.M.. napapata musaganize kuti muyenera kumvelera imodzi mwa nthawizi, koma sankhani nthawi yabwino kwa inu kapena banja lanu. Chofunikira kwambiri ndichakuti, TYAKANI KULIZA.

Zingawoneke ngati zoseketsa, m’mawa uno, kuvala jasi langa papulatifomu, koma ndinali wokondwa—kusonyeza chikhoto chokongola chomwe chalitchi inandipatsa. Ine ndinamuwona M’bale Neville kuno tsiku lina, anavala suti yabwino iyo, momwe iyo inamukwanira iye koma kwambiri, ndipo ine ndinaganiza, chabwino, ine—ine…izo zinawoneka zabwino kwambiri, ndipo osonkhana akulankhula za izo, ine ninaganiza, “Ine Ndingovala chijasi changa papulatifomu.” Ine basi…

Mukudziwa, ndikulupirira kuti sitikula. Nthawi zonse…Ndipo sindikufuna kukula. Nanga bwanji izo, M’bale Luther? Ayi, sindikufuna kukula. Timafuna kukhalaxhabe ana nthawi zonse.

Ambuye akupatseni inu olide lodabwitsa lodzaza ndi Kukhalapo Kwake.

Bro. Joseph Branham

22-1218 Kodi Mulungu Amasintha Konse Malingaliro Ake Pa Mawu Ake?

Uthenga: 65-0418E Kodi Mulungu Amasintha Konse Malingaliro Ake Pa Mawu Ake?

PDF

BranhamTabernacle.org

Okondedwa A Mesiya,

Ndife odzozedwa a Mulungu; wodzozedwa ndi Mzimu Wake womwewo, mwa ntchito zomwezo, mwa Mphamvu zomwezo, mwa zizindikiro zomwezo. Zachoka ku mphungu kupita ku mphungu, zachoka kumawu kupita kumawu, Mpaka kuzulisisa kwa Yesu Kristu kwaonetsedwa mu thupi lathu lililonse, zakuthupi, zauzimu, kapena zofuna zilizonse zomwe tifuna. Mphamvu yofulumizitsa imeneyo ikukhala ndi kukhala mkati mwathu. Ndife a Mesiya a Mulungu.

Mlungu uliwonse Vumbulutso la Uthenga uwu; yemwe ife tiri, kumene ife tinachokera, ndi kumene ife tikupita,kunkala kwachikulu na chikulu. Ife tikudabwa ndi chiyembekezero chachikulu, Iwo angakhoze bwanji kukhala nawo ulemerero winanso? Zingakhale zomveka mochuluka bwanji? Koma ndi tepi yatsopano iliyonse imene timva, Mulungu amalankhula kwa ife milomo ndi khutu ndi kuwulula zambiri za Mawu Ake kwa ife, ndi kutitsimikizira ife,BAMENE IFE.

Chifunisiso chachikulu cha mtima wa wokhulupirira aliyense ndi kukhala mu CHIFUNIRO CHABWINO CHA MULUNGU. Sitikufuna kukhala mu chifuniro Chake chololera. Mitima yathu ndi yosweka ndipo timasweka ngati tiona kuti tachita chilichonse chimene sichingamusangalatse. Tikudziwa kuti Mulungu ali ndi Chifuniro Chabwino, ndipo tifuna kukhala mu PULOGALAMU YAKE YOFUNILA YOKWANIRI.

Mu moyo wanga, ndapanga kaimidwe kolimba ponena kuti ndikulupirira chinthu chofunikira kwambiri chomwe membala aliyense Mkwati angachite, onse wokunva ndi atumiki chimodzimodzi, bafunika KUTYANKA KULIZA. Ndikulupirira kuti Ndi Liwu LOKHA lotsimikizidwa la Mulungu la Tsiku lathu limene muyenera kumva ndi kukulupilila Mawu aliwonse.

Ine ndanena kuti ndikukhulupirira kuti atumiki ayenera kuti amuyike M’bale Branham mumbuyo mu maguwa awo ndi kuliza matepi mu mipingo yawo, popeza Ilo liri Liwu lofunika kwambiri lomwe anthu ayenera kumva.

Ndakhala ndikutsutsidwa kwambiri mumoyo wanga chifukwa choyimirira pazomwe ndimakhulupirira kuti ndi Pulogalamu Yake ndi Chifuniro Chanbwino. Zakhala zosamvetsetseka ndipo zinanenedwa kuti ine sindimakhulupirira mu atumiki asanu wa Aefeso 4.

Ndanena zambiri, nthawi zambiri zomwe ndi zabodza. Sindinanenepo, kapena kukhulupirirepo zimenezo. Pali ambiri omwe apidamula mawu anga ndikuuza anthu zinthu zomwe sindinanene kapena kuzikhulupirira, koma izi ziyenera kuziyembekezera.

Payenera kukhala Mawu a Baibulo Choonadi. Ngati inu mumadzinenera kuti inu mukukhulupirira Uthenga uwu, ndiye ife tiyenera kutenga zomwe mneneri ananena, popeza Iwo uli kutanthauzira komwe kwa Mawu a Mulungu. Pakuti iye ali wotanthauzira YEKHA wa Mawu amenewo.

Ngati tinafunsa aliyense wa inu, “Ndani akufuna kukhala m’chifuniro Chabwino cha Mulungu?”
Aliyense wa inu anganene kuti, “INDE, ndicho chofunisisa cha mtima wanga.” Chifukwa chake tiyenera kuyang’ana ku zomwe mneneri ananena kuti ndi Chifuniro Chabwino cha Mulungu.

WONANI: Ngati Uthenga wa pa tepi suli Mtheradi wanu, ndipo simukulupirira Mawu aliwonse, IMANI KUWERENGA KALATA IYI. Kwa ine, sindinu wokhulupirira, chifukwa chake si zanu. Ine ndikhoza kokha kukhala ndi zomwe Mulungu ananena pa tepi.

Ife tikufuna zomwe Iye ananena; osati zomwe mpingo unanena, zomwe Dokotala Jones ananena, zomwe winawake ananena. Ife tikufuna zomwe PAKUTI ATERO AMBUYE ananena, zomwe Mawu ananena.

Tiyenera kudzipereka tokha ku chifuniro Chake ndi Mawu Ake. Ife sitiyenera kufunsa Iwo. Ife tiyenera kukulupirira Izo. Osati muyesere kupeza njira yozungulira Izo. Tengani Iwo momwe Iwo aliri.

Ambiri amafuna kuyendayenda ndi kupita njira ina. Ngati mutero, Mulungu adzakudalitsani, koma mukugwira ntchito mu Chifuniro Chake cholekerera, osati mu chifuniro Chake chabwino, Chaumulungu. Mulungu adzakulekani inu kuti muchite chinachake, ndipo ngakhale akudalitseni inu pochichita icho, koma icho sichinali chifuniro Chake Chabwino.

Mulungu anatumiza mngelo wake wachisanu ndi chiwiri ku dziko lapansi kuti aitane Mkwati Wake. Ife tikuupirira kuti Uyo anali Mwana wa Munthu akudziulula Yekha mu thupi la munthu. Ndi Liwu lomwe la Mulungu limene lalembedwa ndi kusungidwa kwa Mkwati Wake.

Mulungu Mwiniwake anamuuza mneneri wake, ngati iwe upangitsa anthu kuti akukhulupirire INU, palibe chimene chidzakuimitseni. Iye anali amene anasankhidwa ndi Mulungu kuti atsogolere Mkwati Wake. Palibe amene angatenge malo ake. Ziribe kanthu kuti AKora angati auke bwanji, kapena a Datani angati, anali William Marrion Branham amene Mulungu anamuitana kuti atsogolere Mkwati Wake. Iyi ndi Pulogalamu la Mulungu ndi CHIFUNIRO Chake CHABWINO.

Ngati anthu sangayende mu chifuniro Chake Chabwino, Iye ali nako chifuniro chongololera Iye akulekani inu kuti muyendemo.

Tsopano, Mulungu ndi wabwino…Iye amatumiza Mawu Ake. Ngati inu simudzawakhulupirira Mawu Ake, ndiye Iye amaika mu Mpingo maudindo asanu osiyana: Choyamba, atumwi, aneneri, aphunzitsi, abusa, alaliki. Iwo ali akukwaniritsa Mpingo.

Motero, utumiki unakwezedwa chifukwa chakuti anthu m’mibadwo yonse sanavomereza PULOGALAMU YA CHIFUNIRO CHABWINO CHA MULUNGU; Mawu Ake olankhulidwa ndi mneneri Wake. Ife tiyenera kukhulupirira Mawu amene mneneri wa Mulungu analankhula. Sitifunikira wina aliyense kapena china chilichonse.

Ndiye ntchito ya atumiki ndi kubweretsa anthu kubwerera ku Pulogalamu la Chifuniro Chake Chabwino, lomwe ndi: KHALANI NDI MATEPI, CHIFUKWA CHILI CHIFUNIRO CHABWINO MULUNGU. Kenako sungani CHIFUNIRO CHABWINO PULOGALAMY patsogolo pawo nthawi zonse ndi: KUTYANKA KULIZA.

Inu muyenera kuti mubwerere ndi kuyamba pamene inu munayambira, kapena pamene inu munasiyira, ndi kutenga Mawu wonse a Mulungu.

Ndiye muyenera kuchita chiyani kuti mukhale mu CHIFUNIRO CHAKE CHABWINO: TYAKANI KULIZA.
Kodi abusa ayenera kuchita chiyani kuti akhale mu CHIFUNIRO CHABWINO CHAKE: TYAKANI KULIZA.

Kodi mneneri wa Mulungu anachita chiyani pamene anapita kumisonkhano? Kupempherera odwala, ndi zinthu monga izo? Iye amakhoza kunena zinthu mozungulira kuti nkhosa zimve izo, chifukwa ife tikudziwa chimene Iye akulankhula. Apo ayi, inali nyambo chabe pa mbedza. Iye anawasonyeza iwo zizindikiro monga kuzindikira za mumtima, ndipo ankadziwa zinsinsi za mitima yawo, kuti azingowakoka anthu. Koma kenako ananena kuti chofunika kwambiri chinali:

Chinthu choyamba chimene mukudziwa, tepi imalowa m’nyumba mwawo. Ndi zimenezo, ndiye. Ngati iye ali nkhosa, iye amabwera nayo pomwepo. Ngati iye ndi mbuzi, amathamangitsa tepiyo.

Ndiwe nkhosa kapena mbuzi? Gulu laling’ono la Mulungu lakhazikika pa Mawu amenewo. Tili mu Chifuniro Chake Chanbwino momwe Tikutyanka kuliza monga izo zinali, ndipo ziri, Pulogalamu Lake loyambirira.

Khalani bwino ndi Mawu Ake, chifukwa ndi zomwe ziti zidzatuluke pamapeto pake, Mawu, Mawu ndi Mawu. “Aliyense amene adzachotse Mawu amodzi kwa Iwo, kapena kuwonjezera liwu limodzi kwa Iwo!” Izo ziyenera kukhala, Mawu amenewo.

Ndine wothokoza kwambiri kwa Ambuye kudziwa, mwa Vumbulutso lauzimu, kuti ine ndiri mu Chifuniro Chake Chabwino molingana ndi Mawu Ake. Ine sindikuwonjezera kutanthauzira kwanga kwa Iwo, kapena kumvetsa kwanga kwa Iwo, koma kumva ndi makutu anga omwe chimene chiri PAKUTI ATERO AMBUYE ndi Chifuniro Chake Chabwino.

Ine ndikukuitanani inu kuti mubwere ndi kudzayendera nafe Lamlungu lino pa 2:00 p.m., nthawi ya Jeffersonville, pamene ife tikumva: Kodi Mulungu Amachinja Maganizo Ake Pa Mawu Ake? 65-0418E. Pali zabwino zambiri mu Uthenga uwu, inu mukhala ACHUMA mu Mzimu Wake Woyera tikamaliza.

Bro. Joseph Branham

Eksodo chaputala 19
Numeri 22:31
Mateyu 28:19
Luka 17:30
Chivumbulutso mutu wa 17

22-1211 Uku Ndi Kutuluka Kwa Dzuwa

Uthenga: 65-0418M Uku Ndi Kutuluka Kwa Dzuwa

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Tempele ya mphamvu,

Munthu wakhala ofunisisa mu mtima mwake kukhala ngati Abrahamu pamene anakhala kunyumba kwake cha m’ma 11:00. Atakweza maso anaona amuna atatu akubwera kwa iye anali nadoti ku zovala zawo. Iye anathamangira kwa iwo mwamsanga, ndipo anati, “Ambuye wanga.” Anayima pamenepo pamaso pake, mu thupi laumunthu akuyankhula, anali Melkizedeki Wamkulu.

Lamlungu lino, kufunisisa mu mitima yathu kudzachitika kwa aliyense wa ife. Ife tonse tidzasonkhana pamodzi kuchokera kuzungulira dziko, kumvetsera kwa Melkizedeki wamkulu yemweyo akuyankhula kwa ISE. Munthu wamene analibe bambo, wopanda mayi, wopanda chiyambi cha masiku kapena mathero a moyo, Mulungu, en morphe, amalankhula nafe kupitila mu milomo ya munthu, momwe Iye anachitira tsiku limenelo kwa Abrahamu.

Palibe njira ina yomvera Liwi pokhapokha kuchila KUTYANKA KULIZA. Sipanayambe pakhala nthawi mu mbiriyakale imene Mkwatibwi wakhala akulumikizidwa kuchokera kuzungulira dziko kuti amve Liwu la Melkizedeki likuyankhula pa nthawi yeniyeni yomweyi. Mulungu akugwirizanitsa Mkwatibwi Wake ndi Liwu limenelo.

Ife takhala nawo, kwa zaka, Mawu a Mulungu. Tsopano ife tiri naye Mulungu wa Mawu, mwaona, ndipo pomwe pano akukhala Mawu Ake. Kodi ndi zoona, chimodzi cha zizindikiro zazikulu zotsiriza zimene zalonjezedwa kwa Mpingo Kudza kwa Ambuye kusanachitike.

Lamlungu lino, Mkwatibwi adzakhala ndi Uthenga wa Isita mu Disemba; ndi Uthenga wake womwe ife titi tiumve.

Zimango. Mphamvu. Mphamvu yofulumizitsa. Khristu woukitsidwa. Anawonetseredwa Ana a Mulungu. Mzimu womwewo umene unakhala mwa Khristu ukhala mwa ife. Moyo womwewo, mphamvu zomwezo, opindula omwewo, omwe Iye anali nawo, ife tiri nawo. Ndemanga yachidule. Mbewu yoyamba imene inafika pa kukhwima ikuweyulidwa pamaso pa anthu. Ife tiri tsopano mnofu wa mnofu Wake, fupa la fupa Lake; Moyo wa Moyo Wake, Mphamvu ya Mphamvu Yake! Ndife Iye!

Yesu Kristu woukitsidwayo; Melkizedeki Mwiniwake, adzafuula ndi kutiuza ife, “Ine ndinali ndi Liwu langa litajambulidwa ndipo linaikidwa pa tepi ya maginito kotero kuti ine ndikhoze kukukokerani inu kwa ine, ndipo ine ndikanakhoza kuyankhula kwa inu monga momwe ine ndinachitira Abrahamu. Ndikufuna kuti mumve kuchokera kwa Ine mwachindunji.”

Inu ndinu Mpingo wanga wokonzedweratu, wokonzedweratu! Matupi anu ndiwo kachisi wa Mphamvu, chifukwa kuyambira pachiyambi inu munali gawo la Zimango.

Ndilo vumbulutso Lauzimu lija la Mawu opangidwa thupi. Ngati Iwo unali thupi mu tsiku limenelo mwa Mwana, Mkwati, Iwo ndi thupi lero mwa Mkwatibwi. Mwaona?

Mphamvu yofulumizitsa imeneyo ikukhala mwa ife. Sitiyenera kuopa kalikonse. Mzimu womwewo umene unali mwa Iye, tsopano uli mwa ife ndipo Iwo ukufulumizitsa thupi lathu lachivundi. Sitikuyembekeza choncho, TIKUDZIWA CHONCHO. Ife tinazipanga izo kale, Iye anatipangira izo.

Ndiye, kutsiriza masanawa, Melkizedeki adzayankhula kachiwiri ndi kunena;

Anthu awa, omwe ali mbadwa anzawo a Ufumu, eni ake a Mphamvu yofulumizitsa, afulumizitseni Izo kwa iwo, Ambuye, pakali pano. Ndipo mulole Mzimu upite kuchokera ku mphungu kupita kwa mphungu, kuchokera ku Mawu kupita ku Mawu, mpaka chidzalo cha Yesu Khristu chiwonetseredwe mu thupi lirilonse, kwa thupi, lauzimu, kapena chosowa chirichonse chimene iwo akuchifuna, pamene ife tikuyika manja athu pa modzi. wina. Mu Dzina la Yesu Khristu.

Kuchokera mphungu kupita kwa mphungu, Mawu kupita ku Mawu, chidzalo cha Yesu Khristu chidzawonetseredwa mu lirilonse la matupi athu. ULEMERERO!!

Izi zikhoza kuchitika kokha ndi KUDINISA KULIZA, kodi bwerani mudzajowine nafe ndi kudzatenga nawo gawo mu chisangalalo chazakudya pa Stored Up Food, pamene tikumva Liwu Lija, Lamlungu pa 12:00 p.m., nthawi ya Jeffersonville, kutibweretsera ife Uthenga, Ndiko Kutuluka Kwake. Dzuba 65-0418M.

Bro. Joseph Branham

Malemba

Levitiko 23:9-11
Mateyu 27:51; 28:18
Marko 16:1-2
Luka 17:30; 24:49
Yohane 5:24; 14:12
Machitidwe 10:49; 19:2
Aroma 8:11
1 Atesalonika 4:16
Ahebri 13:8
Chivumbulutso 1:17-18

22-1204 Kodi Melkizedeki Uyu Ndi Ndani?

Uthenga: 65-0221E Kodi Melkizedeki Uyu Ndi Ndani?

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa ganizo la Mulungu,

Ndikukhulupirira kuti mwakonzeka Lamlungu lino. Lankhulani za momwe mitima yathu idzayaka mkati mwathu pamene Iye amalankhula nafe m’njira m’nyumba zathu ndi m’mipingo… Yembekezani!

M’mwezi wathawu watiuza kuti titsimikize kuti takwera chombo choyenera…ndipo tili. Iye anatiuza ife kuti Mbewu yowona ya Mulungu sidzakhala wolandira cholowa ndi mankhusu…ndiye Iye anati, IFE NDIFE Mbewu IYO. Ndiye, tinamva ndi matu athu, Mulungu akulankhula kudzera mwa munthu, natiuza ife, Lero, Lemba ili lakwaniritsidwa pamaso pathu.

Anatiuza Lamlungu lotsatira kuti tiri mu Malo Operekedwa ndi Mulungu Olambirira, ndipo chifukwa ndife, SINACHITE chigololo ndi Mawu Ake. Ndipo, ife ndife Mkwatibwi Wake wa Mawu Namwali Wangwiro.

Lamlungu lino, Iye adzatigwirizanitsa ife tonse pamodzi kachiwiri ndi kulankhula kupyolera mwa mneneri Wake wa mngelo wamkulu ndi kutiuza ife, INE NDINE MELKISEDEKI UYU, ndipo Ine ndikudziulula Inemwini kwa inu mu thupi lamunthu, monga Ine ndinanenera kuti Ine ndidzachita mwa Ine. Mawu.

ULEMERERO! Kodi ndinu okondwa? Kodi ndinu odalisika pupita Mawu? Chabwino, PALI ZAMBIRI ZAKUBWERA. Iye akumaliza nkhani yaikulu imeneyi.

ganizani, IFE tinali mumaganizo a Mulungu kuyambira pachiyambi. Zaka zikwi zinayi Yesu asanabwere padziko lapansi, ndi zaka zikwi zingapo inu musanabwere padziko lapansi, Yesu, mumaganizo a Mulungu, anafera machimo athu. NDIPO, MAYINA ATHU anaikidwa pa Bukhu la Moyo wa Mwanawankhosa.

Kodi izo zikungena m’maganizo mwanu? Mazina athu anadzozedwa ndi Mulungu ndipo anaikidwa pa Bukhu la Moyo wa Mwanawankhosa maziko omwe a dziko asanayikidwe. Iye anadziwa maso athu, msinkhu wathu, chirichonse chimene ife tiri. Ife tinali mu kuganiza Kwake pachiyambi….mu maganizo a Mulungu! Ndiye, chinthu chokha chimene ife tiri ndi Mawu ofotokozedwa a Mulungu. Iye anaziganiza izo, Iye anaziyankhula izo, ndipo ife tiri pano.

Ndizovuta kumvetsa. Mulungu akutiuza ife zinthu zonsezi. Iye amatikonda kwambiri ndipo ankafuna kuonetsetsa kuti tikumva molunjika kuchokera kwa Iye, motero anachititsa kuti lilembedwe Lamlungu, December 4, 2022, kuti abweretsenso Mkwatibwi Wake ndi kutiuza kuti: “Ndinachita zonsezi inu. Ine ndimafuna kuti inu mumve Izo molunjika kuchokera kwa Ine. NDIMAKUKONDANI. IWE NDIWE MKWATI WANGA. NDIKUDZA KWA INU POSACHEDWA.”

Ndicho chifukwa ife timadziwa pamene ife tikuyenda kupita mu Kukhalapo kwa Mulungu, chinachake mwa ife chimatiuza ife kuti ife tinachokera kwinakwake, ndipo ife tikubwerera kachiwiri ndi Mphamvu iyo imene imatikoka ife.

Mulungu wachotsa chigoba pa chinthu chonsecho ndipo ife tikhoza kuchiwona Icho. Mulungu, en morphe, anaphimbidwa mu Lawi la Moto. Mulungu, en morphe, mwa Munthu wotchedwa Yesu. Mulungu, en morphe, mu Mpingo Wake. Mulungu pamwamba pathu, Mulungu nafe, Mulungu mwa ife; kudzichepetsa kwa Mulungu.

Sitiyenera kuopa chilichonse. Palibe chodetsa nkhawa, ngakhale imfa. Pamene tichoka pano, sitinafe nkomwe. Ngati chihema cha padziko chasungunuka, tili ndi chimene chikutidikira, En morphe.

Ine sindingathe kudikira kuti ndimumve Iye akuyankhula kwa ife ndi kuwulula zinthu zonse izi Lamlungu lino pa 12:00 p.M., nthawi ya Jeffersonville. Bwerani mujoine nafe pa malo okhawo omwe mungamve MAWU otsimikiziridwa a MULUNGU akukuuzani inu pakamwa pa makutu kuti Iye ALI ndani, yemwe ife tiri, ndi kumene ife tikupita. KUTYANKA KULIZA.

Kodi Melkizedeki Uyu Ndi Ndani? 65-0221E

Bro. Joseph Branham

Malemba oti muwerenge

Genesis Chaputala 18
Eksodo 33:12-23
Yohane Woyera 1:1
Aroma 8:1
2 Akorinto 5:1
2 Atesalonika 4:13-18
1 Timoteo 3:16; 6:15
Ahebri 7:1-3/13:8
Chivumbulutso 10:1-7; 21:16

22-1127 Chikwati Ndi Chilekano

Uthenga: 65-0221M Chikwati Ndi Chilekano

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Nkhosa za Mneneri,

Kumbukirani, ine ndikunena izi kwa gulu langa lokha. Ndipo kunja pa mphepo, ine ndikunena izi kwa otsatira anga okha. Uthenga uwu uli kwa iwo okha, ndi chimene ine nditi ndinene apa.

Mtumiki aliyense, iye, ameneyo ndi zake, inde, iye ndi m’busa wa gulu la nkhosa, msiyeni iye achite chirichonse chimene iye akufuna. Izo ziri kwa iye ndi Mulungu. Wansembe aliyense, mlaliki aliyense, zili ndi inu, m’bale wanga.

Ine ndikungoyankhula kuno mu Jeffersonville, malo okha amene ine ndingayankhulepo izi, ndi chifukwa ndi nkhosa zanga zomwe. Ndi nkhosa zomwe Mzimu Woyera unandipatsa ine kuti ndizimvetse kuti ndizikhala woyang’anira pa izo, ndipo Iye adzandiimba ine kuyankha pa izo. Ndipo anthu anga awa akhala otembenuka kuno kuchokera ku malo onsewo, amene ine ndawatsogolera kwa Khristu.

Ndi mwala waukulu bwanji kumapeto kwa sabata lakuthokoza. Ndine woyamikira kwambiri kukhala m’gulu la kagulu ka nkhosa kamene kamayang’anirabe ndi aliyense wa inu. Palibe malo ena amene ife tikanapita.

Atate watitumizira ife mphungu yaikulu yowuluka kuti itsogolere Mkwatibwi Wake. Pali malizu ambiri amene amalimbikitsa anthu ndi kulankhula Mawu amene analankhulidwa ndi mneneri Wake, koma pali MAU AMODZI okha amene anatumizidwa kuti atsogolere ndi kuyanjanisa Mkwatibwi Wake.

Mawu amene mneneri wa Mulungu analankhula pa tepi ali Mtheradi wathu. Sitikumvetsedwa chifukwa timati timakhulupirira MAWU ONSE, koma tinalamulidwa ndi mneneri wa Mulungu kuti tichite chimodzimodzi motero

Kotero ndikunena, mu Dzina la Yesu Khristu: Musawonjezere chinthu chimodzi, musatenge, kuika maganizo anuanu mmenemo, inu mumangonena zomwe zanenedwa pa matepi amenewo, inu muzingochita ndendende zomwe Ambuye Mulungu ali nazo. kulamulidwa kuchita; osawonjezera kwa Izo!

Galamukani dziko. Nthawi yayandikira. Mawu amene mneneri wa Mulungu analankhula, MULUNGU ANATILAMULIRA kuti; khulupirirani, kunena ndi kuchita, NDENDENDE zomwe iye ananena pa matepi. Osati zimene ine ndikunena, osati zimene ansembe anu kapena alaliki amanena, koma zimene mneneri wa Mulungu ananena PATEPI.

Palibe china chofunikira kwambiri kuposa kumva Liwu Lija pa tepi, PALIBE. Ife tidzaweruzidwa ndi zomwe zinalankhulidwa PA TEPI. Osati zomwe ine ndinanena, koma zomwe ANANENA.

Ndikufuna ZABWINO KWAMBIRI kwa inu. Mawu anga ochepa ndi okulimbikitsani inu, monga m’busa aliyense ayenera, kuti mukhulupirire Mawu aliwonse. Ine sindimakuphunzitsani inu: kukaikira chirichonse chimene inu mumamva pa tepi, pali zolakwika pa matepi, inu muyenera kuti muzindimva ine mochuluka momwe inu mukuyenera kumumvera mneneri. Ndikukulemberani mawu ochepa okulimbikitsani KUKHALA NDI MAWU OYAMBIRIRA, PRESS PLAY. Ine ndikufuna inu mukhale Mkwatibwi wa Mawu wangwiro, wosadetsedwa.

Mulungu anali ndi Mawu Ake olembedwa mu tsiku ili kotero kuti cholengedwa chamoyo chirichonse chikhoza kumva Liwu Lake. M’masiku a Paulo, iwo anali ndi alembi chabe oti alembe zimene iye anali kulalikira, lomwe ndi Baibulo. Koma LERO, Mulungu anafuna kuti icho chikhale chachikulu koposa. Tikhoza kukanikiza kusewera ndi kumva ndi makutu athu Yesu Khristu woukitsidwayo akulankhula kwa ife, milomo ndi ku khutu.

Ndi tsiku lotani lomwe tikukhalamo. Ndi dziko likugawanika kwenikweni pozungulira ife, tili ndi malo operekedwa omwe tingapiteko ndikungopumula. Timapeza pa TAPE. Khalani m’zipinda zathu zoziziritsa kukhosi ndikudyera Zakudya Zosungidwa Zomwe zasungidwa mosungiramo. Mneneri wathu akhoza kukhala ali patali, koma ife tikukumbukirabe kuti zinthu izi ndi zoona, ndi kuchita monga momwe Mulungu watilamulira ife kuti tichite, KHALANI NDI MATEPI.

Bwerani mukhale ndi phwando lachithokozo labwino kwambiri lomwe munayamba mwadyapo Lamlungu lino pa 12:00 P.M., nthawi ya Jeffersonville, pamene Liwu la Mulungu likulankhula kwa ife Uthenga: Chikwati Ndi Chilekano 65-0221M.

Bro. Joseph Branham

Mateyu 5:31-32 / 16:18 / 19: 1-8 / 28:19
Machitidwe 2:38
Aroma 9:14-23
1 Timoteo 2:9-15
1 Akorinto 7:10-15; 14:34
Ahebri 11:4
Chivumbulutso 10:7
Genesis chaputala 3
Levitiko 21:7
Yobu 14:1-2
Yesaya 53
Ezekieli 44:22

22-1120 Malo Osankhidwa Ndi Mulungu A Kupembedza

Uthenga: 65-0219 Malo Osankhidwa Ndi Mulungu A Kupembedza

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mkazi. Wa Yesu Christu.

Momwe tikondela pa kumva mayina athu ( kuitanidwa) otchedwa. Kungoganiza, ife ndife Amene Iye akuwadzera. Mkwatibwi Wachifumu kwa Mwana wolonjezedwa Wachifumu. Mbewu Yake Yachifumu yapamwamba ya Abrahamu yomwe yakhala yoona ndi yokhulupirika kwa Mawu aliwonse.

Ife sitinachite chigololo, kapena ngakhale kukopana, ndi Mawu ena aliwonse; ife tangodzisunga tokha angwiro ndi kukhala ndi Mawu aliwonse.

Pali akazi ambiri abwino Achikristu mu dziko lero, akazi okhulupirika; koma pali Mayi Mmodzi Yesu Khristu. Ife ndife amene timapita Kwathu ndi Iye. Ndife Mkazi Wake wosankhidwa.

Iye anatiuza ife m’Mawu ake kuti Iye adzabweranso kachiwiri, monga momwe Iye anadzera poyamba. Ndipo apo Iye anayima, akudziulula Yekha mu thupi laumunthu, akuwerenga Mawu ndi kunena kwa ife, “Lero Lemba ili lakwaniritsidwa mmaso mwanu,” ndipo ife tinamuzindikira Iye, ndipo tinakhala Akazi Ake Yesu Khristu Mkwatibwi.

Izo zawululidwa kwa ife kuti mwana mwamuna yemweyo wa Mulungu yemwe anabwera kummawa nadzitsimikizira Yekha monga Mulungu atawonetseredwa mu thupi, ali mwana mwamuna yemweyo yemweyo wa Mulungu mu dziko lakumadzulo, Yemwe wadzizindikiritsa Yekha pakati pa Mkwatibwi Wake. Kuwala kwamadzulo kwa Mwana kwafika.

Ndipo ngati ine nditafunsa funso la chirichonse, payenera kukhala yankho loona. Pakhoza kukhala chinachake pafupi ndi icho; koma payenera kukhala yankho loona, lolunjika ku funso lirilonse. Kotero, chotero, funso lirilonse limene limabwera mu miyoyo yathu, payenera kukhala yankho loona, lolondola.

M’tsiku lathu pali mafunso ndi mikangano yambiri pakati pa anthu.

Kodi kumvetsera matepi a mneneri wa Mulungu kuli kofunika motani?

Ndikofunikira bwanji kumva ndi kukhulupirira Mawu aliwonse?

Mtheradi wathu ndi chiyani? Kodi Ndi zomwe iye ananena pa tepi, kapena kodi Mzimu Woyera umatsogolera munthu aliyense kuti asankhe zomwe ziri ndi zomwe siziri Mawu.

Kodi tiyenera kukhala ndi mwamuna, kapena gulu la amuna, kuti atiphwanyire ife?

Kodi Mawu amati Iye atatha kutumiza Eliya mneneri, Iye adzatumiza gulu la amuna limene liyenera kufotokoza Izo kwa inu?

Kodi ife timasowa winawake kuti atanthauzire Mawu kapena kuwaphwasula Iwo kwa ife?

Kodi tizingomvetsera matepi m’nyumba zathu, m’galimoto, ndi m’malo odzaza mafuta, ndi kumva utumiki pamene tipita ku tchalitchi?

Kodi tizisewera matepi m’mipingo yathu?

Kodi Ndi Liwu la Mulungu la tsiku lathu kapena ayi?

Tsopano, ngati ilo liri funso la Baibulo, ndiye ilo liyenera kukhala nalo yankho la Baibulo. Izo siziyenera kukhala zotheka kuchokera ku gulu la amuna, kuchokera ku chiyanjano chirichonse, kapena kuchokera kwa mphunzitsi wina, kapena kuchokera ku chipembedzo china. Izo ziyenera kubwera molunjika kuchokera mu Lemba…

Choncho ngati tikufuna kupeza mayankho olondola a mafunso athu, tiyenera kuwerenga Malemba. Kenako, tiyenera kusankha amene ali womasulira Malemba mwaumulungu. Kodi munthu aliyense amadzisankhira yekha?

Mneneri amatanthauza osati kungolankhula Mawu, komanso kulosera, ndi Wotanthauzira Waumulungu wa Mawu, Mawu Auzimu olembedwa.

Kotero ngati mneneri ali Wotanthauzira Mwauzimu wa Malemba, ndiye zomwe mneneri ameneyo ananena ndi Mawu a Mulungu kwa Mkwatibwi Wake amene atamasuliridwa kale, NTHAWI.

Izi sizichotsa ku utumiki, kapena udindo umene Mulungu wawaitanira. Iwo aitanidwa ndi Mulungu kusunga Mawu amene analankhulidwa ndi mneneri wa Mulungu pamaso pa nkhosa zawo. Ayenera kuwalozera anthu awo kwa Mtumiki ameneyo ndi Uthenga wa nthawi yake.

Mawu aliwonse amene amalalikira ayenera kuweruzidwa ndi Mawu amene mneneri wa Mulungu ananena pa tepi. Iwo sangakhoze kusintha, ngakhale iwo sangakhoze ngakhale kutanthauzira, MAWU AMODZI. Malemba a Mulungu amatanthauziridwa CHOKHA ndi mneneri Wake.

Tsopano, aliyense wa iwo, ndithudi, ukhoza kuona lingaliro lawo, ndipo ine sindingakhoze kuwadzudzula iwo. Aliyense amadzinenera kuti ndi zoona, ali nacho chowonadi. Ndipo anthu amene ali a mipingo imeneyo ayenera kukhulupirira zimenezo, chifukwa iwo ayika pa—kopita kwawo, kopita kwawo Kwamuyaya, pa kuphunzitsa kwa mpingo umenewo. Ndipo iwo ndi osiyana kwambiri, wina kwa mzake, mpaka izo zimapangitsa mazana asanu ndi anayi ndi chinachake mafunso osiyana.

Ngati Uthenga uwu wolankhulidwa ndi mneneri wa Mulungu suli Mtheradi wanu, koma uli umene munthu wina kapena anthu amanena kuti ndi Mawu, ndiye kopita kwanu Kwamuyaya kukhazikika pa zomwe AKUMANA.

Mawu anga akuwoneka kuti akutsutsana kwathunthu ndi mautumiki onse. sindine. Ine ndikukhulupirira Mulungu waika amuna owona mu Mpingo Wake ndi pamwamba pa zoweta Zake kuti azisunga Uthenga uwu pamaso pawo. Ine ndikukhulupirira iwo amalalikira ndi kukhulupirira Uthenga uwu. Koma chifukwa chiyani iwo sangamuyikenso M’bale Branham mu maguwa awo ngati Liwu lofunika kwambiri kuti amve?

Malaki 3 anati, “Ine ndidzatumiza mtumiki Wanga patsogolo pa nkhope Yanga kuti akonze njira.” Ndipo amene anatumidwa kukakonza njira, anamuzindikiritsa Iye, malowo. “Ndi Iyeyo! Palibe cholakwika. Ndi Iyeyo! Ine ndikuwona chizindikiro chikumutsatira Iye. Ine ndikudziwa kuti ameneyo ndi Iye; Kuwala kutsika kuchokera Kumwamba ndi kubwera pa Iye.” Izo zinali zotsimikizika, ameneyo anali Iye.

Ndiye, m’bale wanga, ine ndikufuna kuti ndikufunseni inu chinachake, potseka. Ife tikhoza kunena izi. Mu Malaki 4, kodi ifenso sitinalonjezedwe mphungu yina, Lawi la Kuwala loti likhale likutsatira, kuti liwusonyeze mpingo wolakwa tsiku lino kuti Iye ali Ahebri 13:8, “yemweyo dzulo, lero, ndi nthawizonse”? Kodi sitinalonjezedwe wina kuti abwere akuuluka kuchokera kuchipululu?

Kodi tiyenera kutsatira chiyani? Lawi la Kuwala lija. Kodi Lawi la Kuwala lija ndi ndani? Mphungu ija, Malaki 4. Ndani anali ndi Lawi la Moto pa mutu wake kuti litsimikizire yemwe iye anali? William Marrion Branham.

Nthawi iliyonse tikasonkhana, tiyenera kusunga Liwu limenelo pamaso pa anthu. Tiyenera kuyika Mau a Mulungu POYAMBA. Osati kumupembedza munthu ameneyo, koma kumupembedzanso Mulungu mwa munthu ameneyo.

Ameneyo ndi mwamuna yemwe Mulungu anamusankha kuti atsogolere Mkwatibwi Wake. Munthu ameneyo ndi munthu amene Mulungu anamusankha kuti azitanthauzira Mawu Ake. Munthu ameneyo ndi munthu amene Mulungu anamusankha kuti amuululire zinsinsi Zake zonse. Munthu ameneyo ndi amene Mulungu anati, “Utengere anthu kuti AKUKHULUPIRIRE,” OSATI MUNTHU WINA KAPENA ZIMENE ENA ANENA, IWE, WILLIAM MARRION BRANHAM. Munthu ameneyo ndi amene adzatidziŵitse za Yesu Khristu.

Mwamuna kapena mkazi aliyense amene amaika chilichonse pa zomwe ndikunena, samakhulupirira zomwe ndikunena.

Bwerani ndi kukhala Akazi a Yesu Khristu nafe Lamlungu lino nthawi ya 12:00 P.M., nthawi ya Jeffersonville, pamene tikumva cholankhulira chosankhidwa ndi Mulungu chikulankhula ndi kutiuza kuti: Malo Osankhika a Mulungu Olambirira 65-0220.

Bro. Joseph Branham

Deuteronomo 16:1-3
Eksodo 12:3-6
Mitu ya Malaki 3 & 4
Luka 17:30
Aroma 8:1
Chivumbulutso 4:7

22-1113 Lero Lembo Ili Lakwanitsidwa

Uthenga: 65-0219 Lero Lembo Ili Lakwanitsidwa

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mbewu Yauzimu Yachifumu ya Abrahamu,

Ndi mpingo uti womwe inu mungapiteko ndi kudziwa, popanda mthunzi wa kukayika, kuti Mawu aliwonse omwe inu mukuwamva ali PAKUTI ATERO AMBUYE? Palibe kulikonse, kupatula ngati inu mukumva Liwu la Mulungu likuyankhula kwa inu pa matepi.

Ndife mphungu za Mulungu ndipo sitidzanyengerera pa Mawu amodzi. Timangofuna Manna atsopano utumiki uliwonse ndipo Iwo sumabwera mwatsopano kuposa kuwamva Iwo molunjika kuchokera kwa Mulungu Mwiniwake. Timawulukira chokwera ndi chokwera pamene tikumva Uthenga uliwonse. Tikamakwera pamwamba, m’pamenenso tikhoza kuona. Ngati mulibe Manna mu mpingo uno, mphungu za Mulungu zikukwezera mmwamba pang’ono mpaka izo zidzawapeza Iwo.

Momwe mitima yathu imalumphira ndi chisangalalo pamene timva Mulungu akuyankhula kwa ife ndi kutiwuza ife kuti ndife ake enieni, obadwa-kachiwiri, Mpingo wa Mulungu, umene umakhulupirira Mawu aliwonse a Mulungu pamaso pa chirichonse, mosasamala chomwe icho chiri, chifukwa ali Mkwatibwi Wake wa Mawu namwali wosaipitsidwa.

Pali chisokonezo choterocho pakati pa anthu lero. Monga mmene zinalili m’masiku a Yesu, otchedwa okhulupirira amenewo anali kutenga kumasulira kwa zimene wansembe ananena ponena za Malemba. Iwo anali kukhulupirira kutanthauzira kwa Mawu kwa munthu. Ndicho chifukwa iwo analephera kuwona Choonadi cha Mulungu, chifukwa panali kutanthauzira kochuluka kopangidwa ndi anthu kwa Mawu a Mulungu. Mulungu samasowa aliyense kuti azitanthauzira Mawu Ake. Iye ali Wodzitanthauzira Yekha.

Kodi inu mukukhulupirira mukanakhala mu nthawi ya Yesu, mukadakhulupirira Mawu aliwonse amene Iye ananena, ziribe kanthu zomwe wansembe wanu ananena? Kodi mukanauza wansembe wanu kuti kumvera Yesu ndiye chinthu chofunika kwambiri chimene mungachite? Kodi mukanamuuza kuti Mawu a Yesu safunikira kutanthauzira? Ngati iwo akanakhala nawo matepi a Yesu akulalikira, kodi mukanamuuza wansembe wanu kuti inu mukufuna kuti iye azisindikiza sewero kotero inu mukhoze kumva ndendende zomwe Yesu ananena ndi momwe Iye ananenera Izo?

Chabwino, umenewo sunali msinkhu wanu; ino ndi m’badwo wanu, ino ndi nthawi yanu. Baibulo linati, Iye ali yemweyo dzulo, lero, ndi kwanthawizonse. Zomwe mukuchita ndi kunena tsopano ndi zomwe mukadachita nthawi imeneyo.

Timakhulupirira kuti mwana mwamuna wa Mulungu yemweyo amene anabwera kummawa ndi kudzitsimikizira Yekha ngati Mulungu atawonetseredwa mu thupi, ndi mwana mwamuna yemweyo wa Mulungu kumadzulo kwa dziko lapansi amene akudzizindikiritsa Yekha pakati pathu. Ife tikukhulupirira lero Lemba ili lakwaniritsidwa pamaso pathu.

Ine ndikukhulupirira moona kuti ichi ndi chaka chovomerezeka, chaka cha chisangalalo. Ngati mukufuna kukhalabe kapolo ndipo osakhulupirira kuti Uthenga uwu uli PAKUTI ATERO AMBUYE; Ngati Uthenga uwu suli Mtheradi wanu; Ngati inu mukukhulupirira kuti zimatengera munthu kuti autanthauzire Uthenga; Ngati inu mukukhulupirira kuti ndi zolakwika kusewera matepi mu mpingo wanu; Pamenepo udzatengedwe, ndipo udzaboola m’khutu mwako ndi nsungulo, ndipo udzamtumikira mbuye wa kapoloyo masiku ako onse.

Koma Mpingo wa Mkwatibwi weniweni ukukhulupirira Mawu onse a Mulungu mu chidzalo Chake ndi mu mphamvu Yake. Ife ndife Mpingo Wosankhidwa umene ukudzikoka ndi kudzipatula ku zinthu zimenezo, ndipo mawonetseredwe a Mulungu akopa chidwi chathu. Ife ndife Mbewu Yauzimu Yachifumu ya Abrahamu.

Ndife oyamikira kuti mwabwera kudzasangalala ndi chiyanjano ichi ndi ife, chomwe tikuyembekezera kuti Mulungu atipatse pa msonkhano uno.

Kotero ife tikukuitanani inu kuti mudzabwere nafe Lamlungu pa 12:00 p.m., nthawi ya Jeffersonville, pamene tikumva 65-0219 Tsiku Lino Lemba Ili Lakwaniritsidwa. Tili pansi pa chiyembekezo chachikulu cha zimene Mulungu akuchita pa misonkhano imeneyi. Kuwala kwamadzulo kwa Mwana kwafika.

Bro. Joseph Branham

Yohane Woyera 16 Mutu
Yesaya 61:1-2
Luka 4:16 St