22-1120 Malo Osankhidwa Ndi Mulungu A Kupembedza

Uthenga: 65-0219 Malo Osankhidwa Ndi Mulungu A Kupembedza

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mkazi. Wa Yesu Christu.

Momwe tikondela pa kumva mayina athu ( kuitanidwa) otchedwa. Kungoganiza, ife ndife Amene Iye akuwadzera. Mkwatibwi Wachifumu kwa Mwana wolonjezedwa Wachifumu. Mbewu Yake Yachifumu yapamwamba ya Abrahamu yomwe yakhala yoona ndi yokhulupirika kwa Mawu aliwonse.

Ife sitinachite chigololo, kapena ngakhale kukopana, ndi Mawu ena aliwonse; ife tangodzisunga tokha angwiro ndi kukhala ndi Mawu aliwonse.

Pali akazi ambiri abwino Achikristu mu dziko lero, akazi okhulupirika; koma pali Mayi Mmodzi Yesu Khristu. Ife ndife amene timapita Kwathu ndi Iye. Ndife Mkazi Wake wosankhidwa.

Iye anatiuza ife m’Mawu ake kuti Iye adzabweranso kachiwiri, monga momwe Iye anadzera poyamba. Ndipo apo Iye anayima, akudziulula Yekha mu thupi laumunthu, akuwerenga Mawu ndi kunena kwa ife, “Lero Lemba ili lakwaniritsidwa mmaso mwanu,” ndipo ife tinamuzindikira Iye, ndipo tinakhala Akazi Ake Yesu Khristu Mkwatibwi.

Izo zawululidwa kwa ife kuti mwana mwamuna yemweyo wa Mulungu yemwe anabwera kummawa nadzitsimikizira Yekha monga Mulungu atawonetseredwa mu thupi, ali mwana mwamuna yemweyo yemweyo wa Mulungu mu dziko lakumadzulo, Yemwe wadzizindikiritsa Yekha pakati pa Mkwatibwi Wake. Kuwala kwamadzulo kwa Mwana kwafika.

Ndipo ngati ine nditafunsa funso la chirichonse, payenera kukhala yankho loona. Pakhoza kukhala chinachake pafupi ndi icho; koma payenera kukhala yankho loona, lolunjika ku funso lirilonse. Kotero, chotero, funso lirilonse limene limabwera mu miyoyo yathu, payenera kukhala yankho loona, lolondola.

M’tsiku lathu pali mafunso ndi mikangano yambiri pakati pa anthu.

Kodi kumvetsera matepi a mneneri wa Mulungu kuli kofunika motani?

Ndikofunikira bwanji kumva ndi kukhulupirira Mawu aliwonse?

Mtheradi wathu ndi chiyani? Kodi Ndi zomwe iye ananena pa tepi, kapena kodi Mzimu Woyera umatsogolera munthu aliyense kuti asankhe zomwe ziri ndi zomwe siziri Mawu.

Kodi tiyenera kukhala ndi mwamuna, kapena gulu la amuna, kuti atiphwanyire ife?

Kodi Mawu amati Iye atatha kutumiza Eliya mneneri, Iye adzatumiza gulu la amuna limene liyenera kufotokoza Izo kwa inu?

Kodi ife timasowa winawake kuti atanthauzire Mawu kapena kuwaphwasula Iwo kwa ife?

Kodi tizingomvetsera matepi m’nyumba zathu, m’galimoto, ndi m’malo odzaza mafuta, ndi kumva utumiki pamene tipita ku tchalitchi?

Kodi tizisewera matepi m’mipingo yathu?

Kodi Ndi Liwu la Mulungu la tsiku lathu kapena ayi?

Tsopano, ngati ilo liri funso la Baibulo, ndiye ilo liyenera kukhala nalo yankho la Baibulo. Izo siziyenera kukhala zotheka kuchokera ku gulu la amuna, kuchokera ku chiyanjano chirichonse, kapena kuchokera kwa mphunzitsi wina, kapena kuchokera ku chipembedzo china. Izo ziyenera kubwera molunjika kuchokera mu Lemba…

Choncho ngati tikufuna kupeza mayankho olondola a mafunso athu, tiyenera kuwerenga Malemba. Kenako, tiyenera kusankha amene ali womasulira Malemba mwaumulungu. Kodi munthu aliyense amadzisankhira yekha?

Mneneri amatanthauza osati kungolankhula Mawu, komanso kulosera, ndi Wotanthauzira Waumulungu wa Mawu, Mawu Auzimu olembedwa.

Kotero ngati mneneri ali Wotanthauzira Mwauzimu wa Malemba, ndiye zomwe mneneri ameneyo ananena ndi Mawu a Mulungu kwa Mkwatibwi Wake amene atamasuliridwa kale, NTHAWI.

Izi sizichotsa ku utumiki, kapena udindo umene Mulungu wawaitanira. Iwo aitanidwa ndi Mulungu kusunga Mawu amene analankhulidwa ndi mneneri wa Mulungu pamaso pa nkhosa zawo. Ayenera kuwalozera anthu awo kwa Mtumiki ameneyo ndi Uthenga wa nthawi yake.

Mawu aliwonse amene amalalikira ayenera kuweruzidwa ndi Mawu amene mneneri wa Mulungu ananena pa tepi. Iwo sangakhoze kusintha, ngakhale iwo sangakhoze ngakhale kutanthauzira, MAWU AMODZI. Malemba a Mulungu amatanthauziridwa CHOKHA ndi mneneri Wake.

Tsopano, aliyense wa iwo, ndithudi, ukhoza kuona lingaliro lawo, ndipo ine sindingakhoze kuwadzudzula iwo. Aliyense amadzinenera kuti ndi zoona, ali nacho chowonadi. Ndipo anthu amene ali a mipingo imeneyo ayenera kukhulupirira zimenezo, chifukwa iwo ayika pa—kopita kwawo, kopita kwawo Kwamuyaya, pa kuphunzitsa kwa mpingo umenewo. Ndipo iwo ndi osiyana kwambiri, wina kwa mzake, mpaka izo zimapangitsa mazana asanu ndi anayi ndi chinachake mafunso osiyana.

Ngati Uthenga uwu wolankhulidwa ndi mneneri wa Mulungu suli Mtheradi wanu, koma uli umene munthu wina kapena anthu amanena kuti ndi Mawu, ndiye kopita kwanu Kwamuyaya kukhazikika pa zomwe AKUMANA.

Mawu anga akuwoneka kuti akutsutsana kwathunthu ndi mautumiki onse. sindine. Ine ndikukhulupirira Mulungu waika amuna owona mu Mpingo Wake ndi pamwamba pa zoweta Zake kuti azisunga Uthenga uwu pamaso pawo. Ine ndikukhulupirira iwo amalalikira ndi kukhulupirira Uthenga uwu. Koma chifukwa chiyani iwo sangamuyikenso M’bale Branham mu maguwa awo ngati Liwu lofunika kwambiri kuti amve?

Malaki 3 anati, “Ine ndidzatumiza mtumiki Wanga patsogolo pa nkhope Yanga kuti akonze njira.” Ndipo amene anatumidwa kukakonza njira, anamuzindikiritsa Iye, malowo. “Ndi Iyeyo! Palibe cholakwika. Ndi Iyeyo! Ine ndikuwona chizindikiro chikumutsatira Iye. Ine ndikudziwa kuti ameneyo ndi Iye; Kuwala kutsika kuchokera Kumwamba ndi kubwera pa Iye.” Izo zinali zotsimikizika, ameneyo anali Iye.

Ndiye, m’bale wanga, ine ndikufuna kuti ndikufunseni inu chinachake, potseka. Ife tikhoza kunena izi. Mu Malaki 4, kodi ifenso sitinalonjezedwe mphungu yina, Lawi la Kuwala loti likhale likutsatira, kuti liwusonyeze mpingo wolakwa tsiku lino kuti Iye ali Ahebri 13:8, “yemweyo dzulo, lero, ndi nthawizonse”? Kodi sitinalonjezedwe wina kuti abwere akuuluka kuchokera kuchipululu?

Kodi tiyenera kutsatira chiyani? Lawi la Kuwala lija. Kodi Lawi la Kuwala lija ndi ndani? Mphungu ija, Malaki 4. Ndani anali ndi Lawi la Moto pa mutu wake kuti litsimikizire yemwe iye anali? William Marrion Branham.

Nthawi iliyonse tikasonkhana, tiyenera kusunga Liwu limenelo pamaso pa anthu. Tiyenera kuyika Mau a Mulungu POYAMBA. Osati kumupembedza munthu ameneyo, koma kumupembedzanso Mulungu mwa munthu ameneyo.

Ameneyo ndi mwamuna yemwe Mulungu anamusankha kuti atsogolere Mkwatibwi Wake. Munthu ameneyo ndi munthu amene Mulungu anamusankha kuti azitanthauzira Mawu Ake. Munthu ameneyo ndi munthu amene Mulungu anamusankha kuti amuululire zinsinsi Zake zonse. Munthu ameneyo ndi amene Mulungu anati, “Utengere anthu kuti AKUKHULUPIRIRE,” OSATI MUNTHU WINA KAPENA ZIMENE ENA ANENA, IWE, WILLIAM MARRION BRANHAM. Munthu ameneyo ndi amene adzatidziŵitse za Yesu Khristu.

Mwamuna kapena mkazi aliyense amene amaika chilichonse pa zomwe ndikunena, samakhulupirira zomwe ndikunena.

Bwerani ndi kukhala Akazi a Yesu Khristu nafe Lamlungu lino nthawi ya 12:00 P.M., nthawi ya Jeffersonville, pamene tikumva cholankhulira chosankhidwa ndi Mulungu chikulankhula ndi kutiuza kuti: Malo Osankhika a Mulungu Olambirira 65-0220.

Bro. Joseph Branham

Deuteronomo 16:1-3
Eksodo 12:3-6
Mitu ya Malaki 3 & 4
Luka 17:30
Aroma 8:1
Chivumbulutso 4:7