22-1113 Lero Lembo Ili Lakwanitsidwa

Uthenga: 65-0219 Lero Lembo Ili Lakwanitsidwa

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mbewu Yauzimu Yachifumu ya Abrahamu,

Ndi mpingo uti womwe inu mungapiteko ndi kudziwa, popanda mthunzi wa kukayika, kuti Mawu aliwonse omwe inu mukuwamva ali PAKUTI ATERO AMBUYE? Palibe kulikonse, kupatula ngati inu mukumva Liwu la Mulungu likuyankhula kwa inu pa matepi.

Ndife mphungu za Mulungu ndipo sitidzanyengerera pa Mawu amodzi. Timangofuna Manna atsopano utumiki uliwonse ndipo Iwo sumabwera mwatsopano kuposa kuwamva Iwo molunjika kuchokera kwa Mulungu Mwiniwake. Timawulukira chokwera ndi chokwera pamene tikumva Uthenga uliwonse. Tikamakwera pamwamba, m’pamenenso tikhoza kuona. Ngati mulibe Manna mu mpingo uno, mphungu za Mulungu zikukwezera mmwamba pang’ono mpaka izo zidzawapeza Iwo.

Momwe mitima yathu imalumphira ndi chisangalalo pamene timva Mulungu akuyankhula kwa ife ndi kutiwuza ife kuti ndife ake enieni, obadwa-kachiwiri, Mpingo wa Mulungu, umene umakhulupirira Mawu aliwonse a Mulungu pamaso pa chirichonse, mosasamala chomwe icho chiri, chifukwa ali Mkwatibwi Wake wa Mawu namwali wosaipitsidwa.

Pali chisokonezo choterocho pakati pa anthu lero. Monga mmene zinalili m’masiku a Yesu, otchedwa okhulupirira amenewo anali kutenga kumasulira kwa zimene wansembe ananena ponena za Malemba. Iwo anali kukhulupirira kutanthauzira kwa Mawu kwa munthu. Ndicho chifukwa iwo analephera kuwona Choonadi cha Mulungu, chifukwa panali kutanthauzira kochuluka kopangidwa ndi anthu kwa Mawu a Mulungu. Mulungu samasowa aliyense kuti azitanthauzira Mawu Ake. Iye ali Wodzitanthauzira Yekha.

Kodi inu mukukhulupirira mukanakhala mu nthawi ya Yesu, mukadakhulupirira Mawu aliwonse amene Iye ananena, ziribe kanthu zomwe wansembe wanu ananena? Kodi mukanauza wansembe wanu kuti kumvera Yesu ndiye chinthu chofunika kwambiri chimene mungachite? Kodi mukanamuuza kuti Mawu a Yesu safunikira kutanthauzira? Ngati iwo akanakhala nawo matepi a Yesu akulalikira, kodi mukanamuuza wansembe wanu kuti inu mukufuna kuti iye azisindikiza sewero kotero inu mukhoze kumva ndendende zomwe Yesu ananena ndi momwe Iye ananenera Izo?

Chabwino, umenewo sunali msinkhu wanu; ino ndi m’badwo wanu, ino ndi nthawi yanu. Baibulo linati, Iye ali yemweyo dzulo, lero, ndi kwanthawizonse. Zomwe mukuchita ndi kunena tsopano ndi zomwe mukadachita nthawi imeneyo.

Timakhulupirira kuti mwana mwamuna wa Mulungu yemweyo amene anabwera kummawa ndi kudzitsimikizira Yekha ngati Mulungu atawonetseredwa mu thupi, ndi mwana mwamuna yemweyo wa Mulungu kumadzulo kwa dziko lapansi amene akudzizindikiritsa Yekha pakati pathu. Ife tikukhulupirira lero Lemba ili lakwaniritsidwa pamaso pathu.

Ine ndikukhulupirira moona kuti ichi ndi chaka chovomerezeka, chaka cha chisangalalo. Ngati mukufuna kukhalabe kapolo ndipo osakhulupirira kuti Uthenga uwu uli PAKUTI ATERO AMBUYE; Ngati Uthenga uwu suli Mtheradi wanu; Ngati inu mukukhulupirira kuti zimatengera munthu kuti autanthauzire Uthenga; Ngati inu mukukhulupirira kuti ndi zolakwika kusewera matepi mu mpingo wanu; Pamenepo udzatengedwe, ndipo udzaboola m’khutu mwako ndi nsungulo, ndipo udzamtumikira mbuye wa kapoloyo masiku ako onse.

Koma Mpingo wa Mkwatibwi weniweni ukukhulupirira Mawu onse a Mulungu mu chidzalo Chake ndi mu mphamvu Yake. Ife ndife Mpingo Wosankhidwa umene ukudzikoka ndi kudzipatula ku zinthu zimenezo, ndipo mawonetseredwe a Mulungu akopa chidwi chathu. Ife ndife Mbewu Yauzimu Yachifumu ya Abrahamu.

Ndife oyamikira kuti mwabwera kudzasangalala ndi chiyanjano ichi ndi ife, chomwe tikuyembekezera kuti Mulungu atipatse pa msonkhano uno.

Kotero ife tikukuitanani inu kuti mudzabwere nafe Lamlungu pa 12:00 p.m., nthawi ya Jeffersonville, pamene tikumva 65-0219 Tsiku Lino Lemba Ili Lakwaniritsidwa. Tili pansi pa chiyembekezo chachikulu cha zimene Mulungu akuchita pa misonkhano imeneyi. Kuwala kwamadzulo kwa Mwana kwafika.

Bro. Joseph Branham

Yohane Woyera 16 Mutu
Yesaya 61:1-2
Luka 4:16 St