Uthenga: 65-0217 Munthu Kuthawa Pamaso Pa Ambuye
- 26-0222 Munthu Kuthawa Pamaso Pa Ambuye
- 24-0526 Munthu Kuthawa Pamaso Pa Ambuye
- 22-1030 Munthu Kuthawa Pamaso Pa Ambuye
Okondedwa Ana A Nkhosa,
Ndi ulemu waukulu komanso mwayi waukulu wotani kunena kuti, “Ndife ana a nkhosa a Mulungu, amene Iye anawatumizira mthenga wake wachisanu ndi chiwiri kuti adzaitane ndikudyetsa Manna Ake osungidwa ndi obisika.”
Ife tikukhutitsidwa ndipo tikukhulupirira kuti Uthenga uwu ndi Liwu la Mulungu lomwe latumizidwa kuti lifikilitse ku ungwiro Mkwatibwi Wake. Ife tikukhulupirira kuti mankhusu akuchoka ku tirigu, ndipo tsopano Mkwatibwi Wake akukhala munkupezeka kwa Mwana, KUKANIKIZA KUSEWERA kuti ache.
Ndipo ndi chimene ife tadzera pano, mzanga, kudzakhala Pamaso pa Mwana kufikira gulu lathu lapang’ono la anthu pano, kufikira litachera kwa Khristu, ilo nkusandulika mkate pa gome Lake. Ndi chimene ine ndikufuna kuti iwo achite.
Aliyense amene sakhulupirira kuti KUKANIKIZA KUSEWERA ndi kumva Liwu la Mulungu lotsimikiziridwa likulankhula kuti ndiye Mawu ofunikira kwambiri omwe muyenera kumva, ndi munthu amene akuthawa pamaso pa Ambuye.
Iwe uyenera kuti ukomane nacho icho, kapena kuchitapo chinachake cha izo. Inu muli nawo udindo, wina aliyense ali nawo, ndipo inu muyenera kukomanizana nazo zinthu izi.
Kodi chobwereza ichi ndi chowona komanso chofunikira bwanji masiku ano. Pali magawano ochuluka pakati pa oitanidwa ake a Mulungu. Kodi ndikofunikira kwambiri kusewera matepi mu tchalitchi kuti mumve Liwu la Mulungu, kapena kodi tsopano ndikofunikira kwambiri kuti utumiki ulalikire Mawu?
Mulungu waitana ndi kuyika utumiki pano kuti usunge Mawu pamaso pa anthu. Iwo ndi Abusa. Mawu amaphunzitsa izi. Iwo ayenera kulemekezedwa ndi kupatsidwa ulemu monga anthu omwe Mulungu wawaitana ndi kuwaika. Ife Sitingathe, ndipo sitiyenera, kunena kuti Iwo si Mkwatibwi. Zimenezo ndi ZOLAKWIKA ndipo sizikugwirizana ndi zomwe mneneri anatiphunzitsa ife. Ine Ndamvapo anthu akunena kuti: “Ngati iwo sakusewera matepi m’matchalitchi awo, iwo ndi otsutsa Mawu.” Inu simukuyenera kunena chinthu monga chimenecho. Zimenezo zikundiwonetsa ine kuti inu muli ndi mzimu wolakwika.
Ndamva ena akunena kuti, “Onse ayenera kumalumikizidwa ndi BT kapena Iwo sali mu chifuniro cha Mulungu”. Inu simukuyenera kunena chinthu monga chimenecho. Mulungu yekha ndiye amadziwa amene ali ndi amene siali Mkwatibwi. Umenewo si mzimu wa Mkwatibwi kunena zinthu monga zimenezo.
Ngakhale ena mwa anthu omwe akulumikizidwa ndi ku BT akunena kuti, “ngati inu mupita kutchalitchi kukamvera matepi ndi kusamavera mu m’nyumba mwanu inu mukulakwitsa!” Zimenezo si zoona abale ndi alongo. Ngati inu mukunena zimenezo, SIYANI, mukulakwitsa. Aliyense ayenera kuchita monga momwe IYE AKUMVELELA KUTSOGOZEDWA NDI AMBUYE MOMWE ACHITIRE.
Atumiki ambiri amaona kuti kulalikira ndiyo njira yoperekedwa ndi Mulungu lero. Ife timangowona zinthu mosiyana, ndiko kulondola. Kodi M’bale Branham ndimochuluka motani anapanga kufanizila uku pa zimenezi? Tamumva pa mafunso ndi mayankho, pamene anthu ankalankhula za M’bale Jackson kuti akulakwitsa, anawadzudzula ponena chilichonse chotsutsana naye ndi mpingo wake.
Ine ndikungolalikira mwa njira ya kalata iyi zomwe ine ndimakhulupirira kuti ndi njira yoperekedwa ndi Mulungu ya Branham Tabernacle. Iwo ndi abale ndi alongo athu. Iwo amakonda Ambuye ndi Uthenga uwu. Umu ndi momwe amamvera kuti Ambuye akuwatsogolera. Ambuye alemekezeke.
Iwo amaziona izo mwanjira ina ndipo ife timazionaso mwa ina, Izo zilibwino. Ine sindingathe kuziona mwanjira yawo ndipo iwo sangaone yanga. Kwa ine, pali njira zambiri zomwe Mulungu wapereka, koma pali NJIRA IMODZI YANGWIRO, NDIPO KWA INE, NDIYO KUMAKANIKIZA KUSEWERA.
Ine ndikupemphera kuti musandive molakwika apa. Kusanjika manja ndi kupempherera anthu ndi zolondola ma peresenti handiredi molingana ndi Mawu. Kudzoza ndi mafuta ndi kupempherera odwala ndi Mawu a Mulungu molingana ndi Malemba. M’bale Branham analalikira ndi kutiphunzitsa ife tonse kukhala Mawu. Koma ine ndikufuna NJIRA YANGWIRO YA MULUNGU YOMWE IYE ANAYIPERELA …. INGOKHULUPIRIRANI CHIFUKWA MULUNGU ANANENA CHONCHO. Ndicho chimene ine ndikuyesetsa kuchita.
Koma tsopano pa machiritso, ndi chifundo cha Mulungu kuti IYE, “Ndi mikwingwirima Yake munachiritsidwa.” Tsopano, choyamba Mawu amanena choncho, zimenezo ziyenera kukhala zokwanira, koma ngati simukukhulupirira mu Mawu, ndiye kuti pali mphatso mu Mpingo, monga amuna omwe ali wodzonzedwa kudziwa momwe angaphunzitsire zimenezo, zomwe zidzapangitsa kuti zikhale zomveka kwa inu, ndiko kuti, ndi chikhulupiriro kukhulupirira.
Ine ndimakhulupirira mu utumiki wofutukuka pasanu. Ndimakhulupirira Mulungu anaitana anthu kuti azilalikira ndi kuphunzitsa Mawu. Koma, ine ndimakhulupirira kuti kumva Liwu la Mulungu pa matepi ndi NJIRA YANGWIRO KWA INE.
Pakumva matepi, ine sindiyenera kumvetsetsa, KUNGOKHULUPIRIRA MAWU ONSE AMENE INE NDIMAMVA. Palibe munthu, palibe mtumiki, palibe malo ena omwe ine ndingapiteko komwe ine ndimakhulupirira MAWU ONSE ndikuyika komwe ndikupita Kwamuyaya, koma matepi.
Kuyambira pachiyambi cha nthawi Mulungu sanapatse anthu ake mwayi ndi luso lodzimvera okha Mawu ake akulankhula milomo ndi khutu. Chinsinsi chilichonse chimawululidwa m’matepi. Funso lililonse limayankhidwa pa matepi. Chilichonse chomwe Mkwatibwi amafunika kuti akhale wangwiro chili pa matepi.
Mawu aliwonse olankhulidwa pa matepi ndi Mawu a Mulungu. Ine sindingamvetse kapena kufotokoza chilichonse, koma ine sindiyenera kutero. Amangofuna kuti ine ndinene AMEN KU MAWU ONSE, ndipo MATEPI ndi malo okhawo omwe ine ndingachite zimenezo.
Koma pamene—pamene iwe uyenera kuchita chinachake chosiyana, pamene iwe uyenera kuti uyime mmene iwe ukumverera kwa chimene iwe ukudziwa kuti ndicho Choonadi, apo ndi pamene pali gawo lovuta, apo ndi pamene kukhula kumabwera, pomwe apo.
Ine ndikukhulupirira kuti ndi zonse zomwe zili mwa ine, tili mu Chifuniro changwiro cha Mulungu ndipo ife tili m’chombo chopita ku Nineve. Ine ndikufuna kuti dziko lapansi libwere kudzayenda nafe pa chombo chathu ndi ife Lamlungu lino nthawi ya 12:00 PM, nthawi ya ku Jeffersonville, pamene ife tikumva Mulungu akulankhula ndi Ana a nkhosa ake.
M’bale Joseph Branham
Uthenga: 65-0217 “Munthu Kuthawa Pamaso Pa Ambuye”
Malemba oti muwerenge:
Yona 1:1-3
Malaki 4
Yohane Woyera 14:12
Luka 17:30