Uthenga: 65-0801M Mulungu Wa M’badwo Woipa Uno
- 26-0531 Mulungu Wa M’badwo Woipa Uno
- 24-0818 Mulungu Wa M’badwo Woipa Uno
- 23-0129 Mulungu Wa M’badwo Woipa Uno
- 21-1003 Mulungu Wa M’badwo Woipa Uno
- 20-0216 Mulungu Wa M’badwo Woipa Uno
Wokondedwa Namwali wamng’ono wa Khristu, Mawu, Gulu la Nkhosa, Mkwatibwi:
Momwe mitima yathu inasangalalira kwambiri titamva mngelo wake wamphamvu akulengeza kuti ndife Mbewu ya Mulungu yokonzedweratu yomwe singachite china chilichonse koma kutsatira Liwu Lake. Izo zimatanthauza zambiri kuposa moyo kwa ife. Inu mukhoza kutenga miyoyo yathu, koma inu simungathe kutenga Liwu Lake. Ife ndife amodzi ndi Mawu Ake. Ife Ndife amodzi ndi Liwu Lake. Ife ndife amodzi ndi Iye.
Izo zikuwoneka zachilendo kwa ife kotero kuti ife sitikumvetsedwa bwino komanso kupangidwa msangulutso chifukwa ife timati timakhulupirira mu nkusewera matepi; kuti ilo ndi Liwu la Mulungu likulankhula ndi Mkwatibwi Wake. Satana ali ndi anthu wanyengedwa kotero iwo amaganiza kuti mwa ife kulengeza kuti ndife mpingo wa tepi, ndi chinthu chinachake chosemphana ndi Mawu, cholakwika, ndipo tikusocheretsedwa, pomwe nthawi zonse Ndi njira yangwiro yoperekedwa ndi Mulungu kwa Mkwatibwi Wake.
Kodi iyo ingakhale njira ina bwanji? Ngati inu mutatanthauzira molakwika Mawu amodzi omwe adalankhulidwa,inu mwatayika.Iwo angakhale ndi chifukwa ndinso cholinga choyenera, koma ndikukhala olakwa. Wina akhoza kudzozedwa ndi Mzimu Woyera koma nkukhalabe wolakwa.
Ngati Mulungu akanakhala kuti sanapereke njira yoti Mkwatibwi Wake amve yekha Mawu onse, ndiye kuti pakanakhala njira ina. Koma Iye wapereka njira kwa munthu aliyense padziko lapansi kuti akhale ndi mwayi womva Mawu akulankhula kwa iwo mwachindunji popanda kufunikira kutanthauzira, kufotokozera, kapena malongosoledwe. Izo zonse ndi Pakuti Atero Ambuye…MFUNDO!
Ife tonse timavomereza kuti tiyenera kukhala ndi Mawu kuti tikhale Mkwatibwi Wake.
Ine ndikukhulupirira kuti chirichonse chimene ife timachisowa chinalembedwa momwemu Umu, zikungosowa kuti zitanthauziridwe ndi Mzimu Woyera. Ine sindikukhulupirira kuti munthu aliyense pa dziko lapansi ali nawo ufulu woika kutanthauzira kwake kwake ku Mawu. Mulungu samasowa aliyense kuti atanthauzire Mawu Ake. Iye ndi Wodzitanthauzira Iye Mwini. Iye anati Iye akanadzachita izo, ndipo Iye akuzichita izo.
Mwachinvekere, Ambuye walankhula ndi kuulula kwa Mkwatibwi Wake kuti palibe njira ina yokhalira Mkwatibwi Wake wosankhidwa koma kukhala ndi Mawu Ake. Mulungu mwiniwake amatanthauzira Mawu Ake Omwe, ndipo palibe wina amene ali ndi ufulu wowonjezera kutanthauzira kwake pa Iwo.
Mawu amanenanso kuti MNENERI Wake ndiye womasulira Mawu Ake. Iye ndi Liwu la Mulungu kwa anthu. Zimene iye amanena ndi Mawu a tsiku lathu.
Mwa kumvetsera Liwu la Mulungu pa matepi, ife timakhala kuti ulosi ukukwaniritsidwa. Palibe china chilichonse champhamvu kwambiri, chopatulika kwambiri, chokwaniritsidwa kwambiri, palibe changwiro kwambiri kuposa kumvetsera Liwu lotsimikiziridwa la Mulungu likulankhula nanu.
Pamene ena anganene kuti palibe chilichonse ku izo, Mphungu zikusonkhana ndikusangalala ndi chisangalalo chachikulu chopitilira, ndi chitsimikizo kuti zikusunga Mawu a Mulungu. Iye anatiuza ife ngati muli ndi makina a tepi, sonkhanitsani gulu la anthu pamodzi, ndipo sewerani iyo, ndipo mvetserani mwatcheru. Mwa chisomo ndi chifundo Chake, ndicho ndendende chomwe ife tikuchita.
Mulungu watiyitana kutitulutsa ife mu m’badwo woyipa uno chifukwa cha Dzina Lake. Ife tikukumana ndi mayeso ndi mayesero ambiri kuposa kale lonse. Satana ali panjira yomenyera nkhondo monga iye akudziwa kuti nthawi yake ili kumapeto. Inu mungakhoze kumadzifunsa nokha kuti, kodi ine ndingamadutse bwanji mu zinthu zonse izi, ndipo Kodi Ine ndine Mkwatibwi Wake?
Inu muli kupangidwa kuwonetseredwa, kuyesedwa, ndi kutsimikizira kwa Satana, NDIFE MKWATIBWI WAKE. Ndife Mawu mu thupi. Ife tikhoza kulankhula Mawu ndipo izo zidzafika pochitika. Izo Ndi PAKUTI ATERO AMBUYE.
Tili ndi Liwu la Mulungu likulankhula mwachindunji kwa Satana ndi kumuuza iye:
Satana, iwe wagonjetsedwa. Iwe ndi wabodza. Ndipo, monga wantchito wa Mulungu, ndi monga antchito, ife tikulamulira kuti mu Dzina la Yesu Khristu, kuti iwe umvere Mawu a Mulungu, ndipo utuluke mwa anthu, chifukwa izo zinalembedwa, “Mu Dzina Langa iwo adzatulutsa ziwanda.”
Chinalichonse …CHINACHILICHONSE chomwe ife takhala tikuchifuna, ife basi timangofunika kupempha, kukhulupirira ndikukhala pomwepo.Izo Zingawonekere nthawi yomweyo; izo zitha kukhala sabata, mwezi, chaka. Izo zilibe kanthu zomwe ife timawona kapena kumvelera, IZO ZINACHITIKAPO MOTERO KALE.
Utumiki uliwonse womwe ife timasonkhana pamodzi umakula ukukulirakulirabe kwa Mphungu za Mulungu. Ife timasonkhana mu lingaliro Limodzi ndi mgwirizano Umodzi, Ife tikukhala pamodzi m’malo Amwambamwamba, tikumvetsera Liwu likulankhula nafe ndikutipanga ife kukhala angwiro ndi Mawu Ake.
Ife tingakonde kuti inu mudzalumikizane nafe Lamlungu lino pa 12:00 masana, nthawi ya ku Jeffersonville, pamene ife tidzamvaso Liwu la Mulungu likulankhula nafe ndikutibweretsera kutanthauzira kwa Mawu Ake Omwe.
M’bale. Joseph Branham
Uthenga: Mulungu Wa M’badwo Woipa Uno 65-0801M
Malemba oti muwerenge musanamve Uthenga
Mateyu Woyera mutu wa 24 / 27:15-23
Luka Woyera 17:30
Yohane Woyera 1:1 / 14:12
Machitidwe 10:47-48
1 Akorinto 4:1-5 / mutu wa 14
2 Akorinto 4:1-6
Agalatiya 1:1-4
Aefeso 2:1-2 / 4:30
2 Atesalonika 2:2-4 / 2:11
Ahebri mutu wa 7
1 Yohane mutu wa 1 / 3:10 / 4:4-5
Chivumbulutso 3:14 / 13:4 / mitu 6-8 ndi 11-12 / 18:1-5
Miyambo 3:5
Yesaya 14:12-14