All posts by admin5

26-0510 Tsiku La Anakubala

Uthenga: 59-0510M Tsiku La Anakubala

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mkwatibwi,

Tsopano, ine ndikuganiza kuti palibe kulemekeza kokwanira kumene tikanakhoza kupereka kwa mayi.

Mayi athu ndiye oyamba nafe, ndipo anapatsidwa udindo waukulu wa zomwe ife tidzakhale komanso njira yomwe ife tiyenera kuyendamo. Iye anapatsidwa udindo kuchokera Kwa Mulungu woti atiyike ife panjira yoyenera. Ndicho chifukwa chake mayi ali nako mwapadela , kukhudza kochepa komwe kwapatsidwa kwa iye kuchokera kwa Mulungu.

Ndi dalitso lapadera bwanji lomwe lili mu nkhokwe la ife la Lamlungu lino, pamene ife tikupereka ulemu kwa Amayi onse, pamene ife tidzamva mngelo wachisanu ndi chiwiri wa Mulungu akufotokoza chikondi ndi ulemu womwe amayi athu ali nawo m’mitima mwathu.

Ife tikudziwa kuti tsiku lililonse ndi Tsiku la Anakubala, koma Lamlungu lino tidzapereka ulemu wapadera kwa Amayi onse pamene ife tidzamva mneneri wathu akupereka ulemu kwa iwo monga momwe iye adayankhula zaka 67 zapitazo pa tsiku lomwelo lofanana , pa 10 Meyi , 1959.

M’bale Joseph Branham

Uthenga: Tsiku la Anakubala 59-0510M

Nthawi: 12:00 P.M. Nthawi ya ku Jeffersonville

Malemba Opatulika: 1 Akorinto 15:1-4

26-0503 Chakudya Chauzimu Mu Nyengo Yake

Uthenga: 65-0718E Chakudya Chauzimu Mu Nyengo Yake

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mkwatibwi,

Liwu lomwe ife tonse timakonda kumva lidzalankhula Lamlungu lino, ndipo lidzatibweretsera ife Uthenga Wapadera wa Kalata Yachikondi, wa Mkwatibwi wa Yesu Khristu yekha.

Liwu limenelo linangolankhula ku dziko lapansi ndikuwachenjeza iwo kuti, “Musayese kundichitira Ine ntchito mopanda kukhala chifuniro Changa. Ndili ndi njira yangwiro yoperekedwa imene ine ndakupangirani inu, Mkwatibwi Wanga. Kumbukirani Mawu Anga, inu muzingonena zimene Ine ndalankhula pa matepi Anga, chifukwa inu mukulowa mu chiweruzo. Chifundo chakanidwa. Koma kondwerani, ndipo khalani oyamikira, chifukwa ine ndapereka ndi kukupatsani inu Chakudya Chobisika, Chakudya Chauzimu, kuti inu mukhale ndi moyo pa ubwino ndi chifundo cha Vumbulutso la Yesu Khristu.

Tsopano muli chilala m’dzikololi lomvera Liwu Langa . Iwo samakumvetsani inu chifukwa inu mumati ndinu anthu a Tepi, ndipo mukufuna kungomva Liwu Langa pa Matepi; koma ndakuitanani kukutulutsani inu ndipo ndakuwululirani inu njira Yanga yangwiro yoperekedwa ya lero.

Inu simunadziphatikize ndi osakhulupirira panthawi ya chilala. Ine ndakupatsani Liwu Langa kuti likuthandizeni. Mwa kusewera Liwu Langa, mgolo wanu siwudzapita wopanda kanthu, ngakhale mtsuko wanu siwudzauma, mpaka tsiku limene ine ndidzabwera ndikukutengani ngati Mkwatibwi wanga.

Ndicho chifukwa chake Ine ndinali ndi Liwu Langa likujambulidwa, kotero kuti inu muKhale ndi malo angwiro operekedwa oti mupiteko, komwe kulibe cholakwika, palibe chifukwa chofuna kutanthauzira, basi Liwu Loyera la Mulungu. Malo omwe mungapiteko kuti mumve ndendende zomwe Ine ndanena: Pakuti Atero Ambuye.

Ine ndidzalankhula nanu momveka bwino Lamlungu.Ine Ndikufuna kuti inu musadzaiwale zomwe ndidzalankhule nanu. Matepi awa ndicho Chakudya Chanu Chauzimu mu Nyengo Ino. Ndi cholemera kwambiri kwa ena a iwo; sangathe kuchidya icho. Icho sichinawululidwe kwa iwo, koma Ine ndakusankhani INU, ndipo ndakupatsani inu Vumbulutso la njira Yanga Yangwiro yoperekedwa.

Kwa inu, Ndi Chakudya Chobisika, komwe mukukhala ndi ubwino ndi chifundo cha Mawu Amoyo.

Pamene Ine ndinali kukhala m’thupi mwa Mwana wanga wa mamuna, iwo mophweka sanathe kuvomereza yemwe ine ndinali: Mulungu ndi munthu. Kenako ine ndinalonjeza kuti ndidzabweranso m’masiku otsiriza ndikukhalanso m’thupi la munthu monga momwe ndinachitira Abrahamu asanakhalepo, ndipo ine ndidzatsika pansi ndikudziveka ndekha m’thupi la munthu monga momwe ine ndinachitira nthawi imeneyo.

Izi ndi zomwe iwo adaphonya, nthawi imeneyo ndi tsopano, koma ine sindikufuna kuti inu muiwale. Chakudya chosungidwa chimene ine ndikukudyetsani inu, ndi mthenga wanga, ndi ofanana. Inu Simungathe kuwalekanitsa iwo. Uthenga ndi mthenga ndi ofanana.Ine ndinakuuzani inu m’Mawu Anga zomwe ndikanachita mu tsiku ili. Ndicho chifukwa chake ndi chifuniro changa kuyika Liwu Langa m’matchalitchi anu, m’nyumba zanu, kulikonse komwe inu mupita; chifukwa ndilo Liwu lofunikira kwambiri lomwe inu muyenera kumva. Ndi Liwu LOKHALO lotsimikiziridwa lomwe limalankhula Pakuti Atero Ambuye.

Chifundo chakhala chikukanidwa. Tsopano inu mukukhala pa Mawu Anga.Ine ndakupatsani inu Vumbulutso la yemwe Ine Ndili ndi yemwe INU muli. Sipayenera kukhala mthunzi umodzi wa kukayika m’mitima ndi m’maganizo mwanu. Inu ndinu Mkwatibwi Wanga Wosankhidwa, Wosankhidwiratu, Wokonzedweratu. Ndinu Mawu Anga Olankhulidwa omwe anali mwa Ine pachiyambi.

Inu muli ndi mwayi wopeza Chakudya, Chakudya Chauzimu, chomwe dziko lapansi silikudziwa kalikonse.

Inu muli ndi mwayi wopeza machiritso a matupi athu pamene madokotala alephera; Ndi chimodzi mwa Zakudya zomwe ine ndinalonjeza ndi kukupatsani inu m’masiku otsiriza.

Ine ndinalonjeza kuulula zinsinsi za mitima yanu ndikuchita izi. Ine ndiri mwa inu. Inu ndinu gawo la Ine, ndipo Ine ndine gawo la inu. Zizindikiro izi zidzawatsata iwo amene akhulupirira.

Lamlungu lino Ine ndidzakhala ndikugwirizanitsa Mkwatibwi Wanga kuchokera kuzungulira pa dziko lonse lapansi ndi Liwu Langa. Ine ndidzakuwuzani inu kuti muyike manja anu pa wina ndi mnzake. Musadzadzipempherere nokha, mudzapempherere amene mwamusanjika manja anu pa iye, chifukwa iwo akukupemphererani inu. Ife tidzapemphera limodzi, ndipo sipadzakhala munthu wofooka kulikonse padziko lonse lapansi ngati inu mudzakhulupirira.

Ngati inu mukhulupirira, ndipo mulibe kukayika mumtima mwanu,Ine ndidzalengeza:

Satana, iwe wagonjetsedwa! Yesu Khristu anakugonjetsa iwe! Iye anawuka kwa akufa ndipo akuyima pakati pa ife usikuuno, kutsimikizira Uthenga uwu wa masiku otsiriza. Tuluka mwa anthu awa! Asiye iwo, mu Dzina la Yesu Khristu! “Mu Dzina Langa iwo adzaturutsa adierekezi,” ndipo iwe watulutsidwa. Mu Dzina la Yesu Khristu asiye osonkhana awa!

Padzakhala machiritso akuchitika kuzungulira pa dziko lonse lapansi kuposa kale lonse.

Ife tikanamayembekezera chifukwa chiyani mwa kutalika kwinanso, m’bale wanga wokondedwa, mlongo, pano Iwo uli, Mzimu Woyera, Mulungu, pano pomwe, chinthu chomwecho ife timachikamba.

Ine ndikuyitana dziko lonse lapansi kuti lidzabwere kudzalumikizana nafe Lamlungu lino pa 12:00 PM, nthawi ya ku Jeffersonville, ndikudzamva Uthenga ndi mthenga Wake akutibweretsera ife Chakudya Chauzimu Mu Nyengo Yake, Chakudya Chobisika cha Mkwatibwi.

M’bale Joseph Branham

Uthenga:  Chakudya Chauzimu Mu Nyengo Yake 65-0718E 

Mthenga: M’busa . William Marrion Branham

Malemba Opatulika: 1 Mafumu 17:1-7 / Amosi 3:7 / Yoweli 2:28 / Malaki 4:4 / Luka 17:30 / Yohane Woyera 14:12

26-0426 Kuyesa Kuti Umuchitire Mulungu Ntchito Mopanda Kukhala Chifuniro Cha Mulungu

Uthenga: 65-0718M Kuyesa Kuti Umuchitire Mulungu Ntchito Mopanda Kukhala Chifuniro Cha Mulungu

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mkwatibwi Wosamalidwa,

Ola lachedwa. Nthawi yafika. Chisankho chiyenera kupangidwa. Mulungu akuchenjeza ana Ake. Ambuye Mulungu wathu walengeza ndi kutsimikizira kwa ife chomwe Choonadi Chake chili ndi Mawu Ake, ndi Mzimu Wake. Osati ndi mphamvu, osati ndi nkhondo, koma ndi Mzimu Wanga, ndipo Mawu Anu ndi Choonadi.

Iye watsimikizira kwathunthu kwa Mkwatibwi lero kuti Yesu Khristu ali yemweyo dzulo, lero, ndi nthawi zonse.Iye watiwonetsa ndi kutiwululira kuti Uthenga ndi mthenga wa ora ali ofanana. Iye wativumbulutsira zinsinsi Zake zonse zomwe zinali zobisika mu Mawu. Iye watitsimikizira Izi ndi Mzimu Wake Woyera. Palibe funso m’maganizo mwathu, m’mitima kapena m’miyoyo yathu. Mawu Ake pa matepi ndi PAKUTI ATERO AMBUYE KWA MKWATIBWI WAKE.

Mulungu nthawi zonse walola njira zambiri kubwera kwa Iye.Iye amapanga chifuniro Chake chongololera kukhala chifuniro Chake Changwiro. Iye mongaso nthawi zonse wapereka CHIFUNIRO CHANGWIRO NDI NJIRA YABWINO KWA ANA AKE. Ambiri amayesa kubwera mwanjira yosiyana pochitira Mulungu ntchito popanda kukhala chifuniro Chake changwiro.Izo Zingawonekere ndikumveka ngati chifuniro Chake changwiro, koma izo sizili monga ndi Mawu Ake.

Ngakhale munthu wamkulu, wodzozedwa kumene, wochokera ku Kukhalapo kwa Mulungu, adapeza vumbulutso loti achite china chake kwa Mulungu, ndipo amafuna kuchichitira Mulungu; koma vumbulutso lomwe anali nalo linali lolakwika.

Aliyense wa ife ayenera kupeza njira Yake yangwiro yoperekedwa. Kodi ife tingadziwe bwanji kuti tili mu chifuniro Chake changwiro ngati wina wodzozedwadi, wochokera ku kukhalapo kwa Mulungu, ndi vumbulutso, si ali mu chifuniro changwiro cha Mulungu?

Pali NJIRA IMODZI YOKHA YODZIWIRA YA CHOWONADI, ndipo Mulungu wapereka njira imeneyo kwa Mkwatibwi Wake.

Liwu la Mulungu Mwiniwake lawuza mpingo uno, ndi inu nonse anthu omwe muli pa matepi, ndi anthu omwe ali olumikizidwa pa intaneti m’madera ena a dziko lapansi, nthawi imeneyo ndi TSOPANO. Iye anatiuza ife kuti timvere mwatcheru Kwambiri zomwe iye anali kunena , ndipo kuti ife TISALEPHERE.

Chotero ine ndikunena, mu Dzina la Yesu Khristu! Musati inu muwonjezere kanthu kamodzi. Musati mutenge, kuyika malingaliro anu omwe mwa Iwo. Inu muzingonena chimene chikunenedwa pa matepi awo. Inu muzingochita chimodzimodzi chimene Ambuye Mulungu wakulamulirani kuti muchite. Musati muwonjezere kwa Iwo.

Iye sananene kuti, ndipo izo sizikutanthauza kuti alaliki sangalalikire Mawu, aphunzitsi sangaphunzitse Mawu, kapena abusa kapena aneneri ife tichite zomwe tayitanidwira kuchita; iwo ayenera, ine ndiyenera.Ife tayitanidwa ndi kudzozedwa kuti tichite zimenezo.Ife tiyenera kuloza ndi kubwereza Uthenga uwu ndi mthenga kwa anthu, chifukwa iwo ndiwo Mawu a tsiku lathu.

Koma Iye akutiuza momveka bwino kuti tonsefe a ife tikhoza kudzozedwa, ndi kudzozedwa kolondola, kudzazidwa ndi Mzimu Wake Woyera, ndi vumbulutso latsopano, ndikukhala kunja Kwa chifuniro Chake. Mu tsiku lathu lino, Iye wapereka NJIRA YANGWIRO yodziwira motsimikiza kuti mukumva Liwu la Mulungu, lochokera kwa Mulungu Mwiniwake. Ndiyo njira YOKHAYO yangwiro.

Utumiki suyenera kungotchula mobwereza kokha ndi kulalikira Uthenga uwu, koma ife tiyenera kusewera Liwu la Mulungu pa matepi kwa anthu. Palibe KUDZOZA KWAKUKULU kuposa kumva Liwu la Mulungu. Palibe njira ina yodziwira popanda mthuzi wa kukayikira kuti zomwe ife tikumva ndi NDIZOMWEZODI zomwe Mulungu ananena.

Mu tsiku lino, mosiyana ndi tsiku lina lililonse mu mbiri ya dziko lapansi, Mulungu wapereka njira yomwe imapangitsa kuti zikhale zosatheka kuphonya izo, ngati inu ndinu Mkwatibwi Wake Wokonzedweratu.Iyo yatsimikiziridwa ndi kuwululidwa ndi Lawi la Moto Mwiniwake kuti ndi Liwu la Mulungu Mwiniwake likulankhula mwachindunji ku Mpingo Wake.

Kwa zaka zikwizikwi, ana a Mulungu akhala akulakalaka ndikukhala nayo njala yakumva Liwu la Mulungu pa Iwo eni.Momwe iwo bwanji anakhumba akanakhalapo tsiku limene lija pamene Yesu analalikira kwa zikwizikwi paphiri. Kumva momwe Iye analankhulira Mawu Ake mwachikondi ndi chifundo. Kumva momwe Iye anayikila kutsimikiza pa Mawu aliwonse. Momwe Iye analankhulira ndi kulimbikitsa mitima yawo.

Ife tili amoyo tsopano ndipo tili mu mkupezeka kwa Mulungu kumva Liwu la Mulungu.

Tsiku lina posachedwa sitidzabwerera ku moyo wamtundu uwu kachiwiri. Tidzabwerera ngati munthu wosafa. Uchimo udzachotsedwa. Satana adzamangidwa kwa zaka chikwi ndipo tidzakhala padziko lapansi lino lomwe Ambuye Mulungu wathu watipatsa.

Ife ndife athunthu handiredi peresenti. Ife sitidakhalepo osangalala kapena mochuluka osakhalapo ndi mafunso m’miyoyo yathu. Ife ndife mmodzi ndi Iye ndi Mawu Ake. Ife ndife Mawu Ake. IFE TILI MU CHIFUNIRO CHAKE CHANGWIRO MWAKUKHALABE NDI LIWU LAKE, MAWU AKE. Iye adzabweranso tsiku lina lililonse tsopano kuti adzatitenge ife limodzi naye.

Zikomo inu Ambuye Yesu!

Ambuye Mulungu wanu wawonetsera kwa inu chomwe chiri Choonadi. Ambuye Mulungu wanu watsimikizira chomwe chiri Choonadi, mwa Mawu Ake ndi mwa Mzimu Wake. “Si mwa mphamvu, si mwa nkhondo, koma mwa Mzimu Wanga.” Ndipo, Mzimu, “Mulungu akufuna iwo amene ampembedza Iye mu Mzimu ndi Choonadi.” “Mawu Anu ali Choonadi.” Ndipo Iye watsimikizira mwathunthu kuti Yesu Khristu ali yemweyo dzulo, lero, ndi nthawizonse. Iye wawonetsera Mbewu ya madzulo kwa inu. Iye wawululira Iyo kwa inu, mu Mawu. Iye wayitsimikizira Iyo kwa inu, mwa Mzimu Wake.

Ndi mtima wanga wonse ine ndikukuitanani aliyense wa inu kuti mubwere kudzalumikana ndi gawo la Mkwatibwi Wake pamene tikulumikizana kuchokera padziko lonse lapansi nthawi ya 12:00 PM, nthawi ya ku Jeffersonville, kuti tidzamve Liwu Lake likulankhula kudzera mwa mthenga wake wachisanu ndi chiwiri wa mngelo ndikutibweretsera ife Uthenga: Kuyesa Kuti Umuchitire Mulungu Ntchito Mopanda Kukhala Chifuniro cha Mulungu 65-0718M.

M’bale Joseph Branham

Malemba Owerenga Musanamve Uthenga:
Deuteronomo 4:1-4 / 4:25-26
1 Mbiri 13
1 Mbiri 15:15
Masalimo 22
Mariko Woyera 7:7
Yoweli 2:28
Amosi 3:7
Malaki 3
Mateyu Woyera 11:1-15
1 Akorinto 13:1

26-0419 Kusankha Kwa Mkwatibwi

Uthenga: 65-0429E Kusankha Kwa Mkwatibwi

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mkwatibwi Wosankhidwa,

Pamene ife tikumvetsera Uthenga uwu, Kusankha Kwa Mkwatibwi, ena amaganiza kuti mneneri akungolankhula ndi kutilangiza za khalidwe ndi thunthu limene mwamuna ayenera kuyang’ana akamasankha mkazi amene akufuna kukhala mkazi wake. Izo ndi zoona, iye akutero, koma pali kalata yeniyeni yobisika yachikondi m’Mawu Ake. Zimene Iye akuulula kwa Mkwatibwi Wake ndi zozama kwambiri. Mulungu akulankhula ndi iye mwachindunji, kumuuza zomwe ankafuna mwa Iye, ndi chifukwa chake Iye anamusankha iye kuchokera pachiyambi. Iye anafuna kuti Iye adziwe kuti wamusankha iye kukhala MKWATIBWI WAKE WOKONDEDWA WOKOMA MTIMA yemwe Iye ankafuna kugawana naye Umuyaya Wake.

Pachiyambi, Mulungu anali kufunafuna Mkwatibwi amene adzakhala ndi Khalidwe Lake lomwelo. Mzimu Wake womwewo ukanadzaonekera mwa Iye. Iye anafuna Mkwatibwi amene akanadzakhala wodzipereka kwambiri kwa Iye, ndi Mawu Ake olonjezedwa,Kufikira mpaka Maganizo omwe anali mwa Iye adzakhale mwa Iye. Iye ayenera kuumbidwa monga momwe Iye alili.

Iye anafuna kuti Iye akhale thupi Lake lomwelo, mafupa omwewo, Mzimu womwewo, chilichonse chomwecho, basi chimodzimodzi monga Iye. Awiriwa a iwo adzakhala M’MODZI.

Iye sakanakhala wa chimasomaso mmaso mwake . Iye sakananyengereredwa ndi ma liwu ena aliwonse. Iye akanakhala woona mtima komanso wokhulupirika kwa Iye, mosasamala kanthu za zomwe wina anganene. Iye akanamutenga Iye pa Mawu Ake. Chilichonse chimene Iye adanena, AKANAKHULUPIlIRA MAWU ONSE, zilibe kanthu kaya ndi motalika bwanji zingatenge kuti zikwaniritsidwe, iye Akanakhulupirira izo. Iye akanakhalabe ndi Mawu Ake.

Iye akanakonda Iye, ndipo Iye yekhayo. Iye sanafunikire kumupatsa iye chuma chambiri, iye anali ndi Ngale yamtengo wapatali, Vumbulutso lenileni la Iye. Iye akanadziwa, iwo anali M’MODZI ndipo ndi ofanana. Mzimu Wake ukanakhala mwa Iye. Chilichonse chimene Iye akanafuna, Iye akanamupatsa Iye; chomwe Iye ankayenera kuchita chinali kupempha ndi kukhulupirira, ndipo Iye akanachita icho.

Iye ankadziwa kuti Iye akanapita kwa nthawi yaitali kuti akamumangire nyumba yomwe ikanakhala ndi chilichonse chofanana ndi Iye. Iye ankayimanga iyo momwe Iye akanakondera. Iye ankadziwa tsiku lina Iye adzabweranso kwa Iye, monga momwe Iye analonjezera, ndiye kuti adzakhala ndi Mgonero Waukwati waukulu kwa zaka chikwi. Kenako, adzapita limodzi ku Nyumba yokongola imene Iye adamumangira iye kuti akhale Kwamuyaya.

Palibe china chilichonse chomwe chingakhale chovuta kwa Iye. Iye Sadzafuna china chilichonse. Iye adzakhala choncho wokhutira ndi wokhutsidwa ndi pokhala ndi Vumbulutso podziwa yemwe Iye ali, ndi kuti Iye ndi ndani. Iye anadziwa kuti Iye adzasunga Mawu Ake. IYE ADZAKWANIRITSIDWA, PODZIWA KUTI IYE NDIYE YOMWE IYE ANASANKHA KUTI AKHALE MKWATIBWI WAKE.

Abale ndi alongo anga, Mulungu wamphamvu wa Kumwamba ndi dziko lapansi anayang’ana kupitilira mumuyaya ndipo WAKUSANKHANI… INU KUKHALA MKWATIBWI WAKE WOSANKHIDWA WOKOMA MTIMA.

Ine ndikukuitanani inu kuti mubwere mudzalumikizane nane limodzi ndi gawo la Mkwatibwi Wake Lamlungu lino, pamene Iye akulankhula kudzera mwa mngelo wake wamphamvu ndikutiuza kuti ndife Mkwatibwi Wake Wosankhidwa.

M’bale Joseph Branham

Uthenga:   65-0429E  Kusankha Kwa Mkwatibwi
Nthawi: 12:00 P.M. Nthawi ya ku Jeffersonville

Malemba:
Genesis 24:12-14
Yesaya 53:2
Chivumbulutso 21:9

26-0412 Kodi Mulungu Amasintha Konse Malingaliro Ake Pa Mawu Ake?

Uthenga: 65-0418E Kodi Mulungu Amasintha Konse Malingaliro Ake Pa Mawu Ake?

PDF

BranhamTabernacle.org

Okondedwa Iwo Ofulumizitsidwa,

Momwe mitima yathu inakondwera monga Mphungu kumapeto kwa sabata ino ya Isitala. Tsiku ndi tsiku, kudzoza kwake kunali kukukulirakulirabe kwambiri. Mgonero, Kuikidwa m’manda, Ungwiro, kenako chimake chachikulu chomwe Iye anatiwumbirako: Ndikutuluka kwa Dzuwa…ULEMERERO, IYE WAUKA ndipo ali ndi moyo mwa aliyense wa ife. Iye anali kuulula Mawu Ake kwa aliyense wa ife monga momwe sitinamvepo kale. Kudzoza kunadzaza mitima yathu, kukhalapo kwake kunadzaza mlengalenga; zinkaoneka ngati Kukwatulidwa kunali pafupi.

Iye anatiuza zomwe zinachitika zaka 2000 zapitazo, kenako zomwe zinali kuchitika mu 2026. Yesu anali Mbewu yoyamba ya Tirigu wa Mulungu yomwe inaukitsidwa kwa akufa. Iye anaukitsidwa ndi Mphamvu ya Mulungu yofulumizitsa. Mulungu anafulumizitsa moyo Wake, anamuukitsa Iye kwa akufa, ndipo Iye anali zipatso zoyamba za iwo omwe anagona. Anali woyamba kufika kukucha, Mtolo wa Mulungu womwe unaweyulidwa ngati chikumbutso cha kuyamika Mulungu, kukhulupirira kuti enafe tidzabwera. Icho chinali chizindikiro.

KENAKO IYE ANATIWULULIRA ZIMENE ZILI KUCHITIKA LERO. Monga momwe Iye anaweyulidwa pa Tsiku la Pentekoste pamene kunamveka mkokomo wochokera Kumwamba ngati kuweyula, mphepo yamphamvu yothamanga ikuweyulira pa anthu. Inaweyulidwiranso pamwamba pa anthu monga momwe Iye analonjezera mu Luka 17:30 ndi Malaki 4, pamene M-w-a-n wa munthu adzawululidwa ndi kuweyulidwanso pa anthu.

Tsopano, Mwana wa munthu ndi Ndani? “Pachiyambi panali Mawu, ndipo Mawu anali ndi Mulungu, ndipo Mawu anali Mulungu. Ndipo Mawu anasandulika thupi, ndipo anadzakhala pakati pathu.” Ndipo ngati kuphunzitsa konse kumene ife tiri nako, ndi kutsimikizira kwa Mawu a Mulungu; mwa Mawu a Mulungu, mwa zizindikiro, ndi zodabwitsa, ife tikuziwona lero, kuti mu Bukhu la—la Luka apa, kuti monga ife tangobwereza kumene, kapena—Luka mutu wa 17 ndi ndime ya 30; ndi Malaki 4, ndi Malemba osiyanasiyana amene ife tikuwadziwa, kuti Mawu amenewo akuweyulidwanso pa anthu, kuti miyambo yakufa ya anthu yafa, ndipo Mwana wa Mulungu ali moyo kachiwiri ndi ubatizo wa Mzimu Woyera pakati pathu pomwe, ndipo akutipatsa ife Moyo.

Mzimu Woyera unapitirizabe kuweyulira ndi kuweyulirabe, kuulula ndi kuulula Mawu Ake… Mphamvu, machitidwe, Mphamvu yofulumizitsa…

Kenako, pamene zinaoneka ngati sizingakule kwambiri, Iye anatiuza kuti:

Iye anandilola ine kuyang’ana kudutsa katani, ndipo ine ndinakuonani inu nonse kumeneko. “Onse amene iwe unawakonda, ndi onse amene anakukonda iwe, iwo aperekedwa kwa iwe.” Mukuona? Ine ndinawawona iwo paliponse kumeneko monga choncho. Chinali chiyani chimenecho? Mphamvu Yofulumizitsa.

IYE ANATIONA IFE KUMENEKO!! Kupitirira katani ya nthawi….ife tinali KUMENEKO ndi iye; okondedwa athu onse omwe adatsogola…abambo, amayi, ana. Ife tidali nawo pamodzi ndi onse omwe sitinakumanenawopo: Mose, Eliya, Petro, Paulo….tinali tonse pamodzi.

Kenako, monga momwe basi wokondedwa Mzimu Woyera Iye ali wokongola, Iye sankafuna kutiiwala ife odwala, ovutika maganizo komanso omenyedwa, choncho Iye anadziweyula iyemwini pa ife kuti aliyense achiritsidwe ku chilichonse chomwe tinkachifuna.

Anthu awa, amene ali nzika zimzathu za Ufumu, eni a Mphamvu zofulumizitsa, fulumizitsani Iyo kwa iwo, Ambuye, pakali pano. Ndipo mulole Mzimu upite kuchokera kwa mphungu kupita kwa mphungu, kuchokera ku Mawu kupita ku Mawu, mpaka chidzalo cha Yesu Khristu chitawonetseredwa mu thupi lirilonse, ku zakuthupi, zauzimu, kapena chosowa chirichonse chimene iwo akuchisowa, pamene ife tikuyikana manja athu pa wina ndi mzake. Mu Dzina la Yesu Khristu.

Mawu amenewo. Liwu limenelo. CHILICHONSE chimene ife tikufuna chili pa matepi, Mkwatibwi. Mulungu sasintha malingaliro ake pa Mawu Ake. Palibe dontho limodzi kapena Mutu umodzi omwe ungasinthidwe, kotero Iye anapanga njira kuti Mkwatibwi Wake amve NDENDENDE ndi makutu awo chimene Iye amafuna alankhule Kwa iwo.

Mulungu walankhula ndi Mkwatibwi Wake ndipo wawulula CHILICHONSE. Izo zili zojambulidwa. Mkwatibwi ayenera kubwera kwa Mkwati; Iyo ndiyo njira Yake yangwiro yoperekedwa yomwe yapangidwira lero.Izo ndi PAKUTI ATERO AMBUYE.

Kodi Mulungu amasintha konse malingaliro Ake pa Mawu Ake? AYI. Iye ali ndi CHIFUNIRO CHANGWIRO NDI CHIFUNIRO CHONGOLOLERA. Mkwatibwi ayenera kukhala mu CHIFUNIRO Chake CHANGWIRO. Palibe Chifuniro changwiro china, kapena malo angwiro, kuposa kumva Liwu la Mulungu mwachindunji kuchokera kwa Mulungu Mwiniwake.

Kuitana kwanga kwa wina aliyense wa inu ndikuti mudzalumikizane nafe Lamlungu pa 12:00 PM, nthawi ya ku Jeffersonville, kudzanva Liwu la Mulungu likutibweretsera Mawu Oyera. Palibe kufunikira koganizira, kungokhala kumbuyo basi ndi kumanena AMEN KU MAWU ALIWONSE….palibe malo ena omwe zingachitikire, ndi kokha mwa KUKANIKIZA KUSEWERA.

M’bale Joseph Branham.

Uthenga: 65-0418E — Kodi Mulungu Amasintha Konse Malingaliro Ake pa Mawu Ake?

Tiyamba ndi ndime 61.

Malemba Oti muwerenge musanamve Uthenga:
Eksodo mutu wa 19
Numeri 22:31
Mateyu Woyera 28:19
Luka 17:30
Chivumbulutso mutu wa 17

ISITALA 2026- MWAMBO WA MGONERO WA PADELA NDI KUSAMBITSANA MAPAZI

Okondedwa Azanga Nzika Za Ufumu,

Isitala iyi ikulonjeza kukhala Isitala yayikulu kwambiri yomwe Mkwatibwi adakhalapo nayo. Ife Takhala tikukhala pamaso pa Mwana, tikucha, tikuzindikira kuti ndife ndani. Chidzalo cha Yesu Khristu chikupangidwa kuonetseredwa mwa wina aliyense wa ife pamene Mawu Ake, Liwu Lake, likufuula, kuchokera Kwa Mphungu yaikulu kupita kwa ti ana ta mphungu, kutiitana ife ku Mgonero Wathu wa Ukwati.

Chaka chilichonse nthawi ino Mkwatibwi amakhala pansi pa kuyembekezera kwakukulu kwa Isitala ilimkudza kumapeto kwa sabata. Nthawi yomwe Iye adzatigwirizanitsa kuchokera padziko lonse lapansi kwa masiku anayi mopitiliza, kumulambira Iye, kumuyamika Iye, kumutamanda Iye; chifukwa Iye wauka ndipo akukhala mwa wina aliyense wa ife. Mkwati ndi Mkwatibwi akukhala M’MODZI.

Iye akutipatsa ife nthawi yapaderayi kuti titsekere kunja zinthu zonse za dziko lapansi zomwe zatizungulira ife ndikukhala basi ndi Iye . Palibe zosokoneza za dziko lino, pamene tikupanga dziko lathu ndi Iye. Tsekani zitseko zathu, zimitsani zathu zonse zamagetsi ndi chilichonse chomwe chimatisokoneza kwa Iye.

Chikhumbo chachikulu chomwe wina aliyense wa ife ali nacho ndikukhala pafupi ndi Iye. Ife tikufuna kukhala moyo wodzipereka kwambiri kwa Iye; kukhala nthawi zonse mu chifuniro Chake changwiro. Kukhala okonzeka Kukubwera Kwake. Palibe chilichonse m’dziko lino, kapena m’moyo wathu, chofunika kwambiri kuposa ichi.

Iye watipatsa mwayi wapaderawu kuti tingokhala ndi Iye, kulankhula ndi kusinkhasinkha za Iye. Kukhala pamaso Pake ndikutsegula mitima yathu kwa Iye. IZO ZIDZAKHALA ZOSINTHA MOYO KWA MKWATIBWI WAKE!

Iye akudziwa kuti zingakhale zovuta kwa ena a inu omwe muli ndi ana, banja, ndi maudindo ena omwe tili nawo, koma ngati tigwiritsa ntchito mphindi iliyonse yaulere tiyenera kulankhula ndi Iye, kuyandikira kwa Iye, kutsegula mitima yathu kwa Iye, padzakhala kusintha kwakukulu mu kuyenda kwathu ndi Iye, mpaka sitidzakhalanso chimodzimodzi.

Monga momwe Iye adachitira m’tsiku la Mose pamene Iye adawakhazika ana Ake m’nyumba zawo, magazi anali atapakidwa ndipo anali kudzipangitsa Iwo eni kukonzekera Kutuluka kwawo; momwemonso sabata yapadera iyi ya Isitala yomwe Iye adakonza idzakhala ya aliyense wa ife.

Ulendo wathu udzakhala motere:

LACHINAYI

Unali Lachinayi usiku pamene Ambuye Yesu adadya Mgonero Womaliza ndi ophunzira Ake, pokumbukira Paskha asanatuluke ana a Israeli. Ndi mwayi waukulu bwanji womwe ife tili nawo wolankhulana ndi Ambuye m’nyumba zathu, kumapeto kwa sabata yathu yopatulika, ndikupempha Iye kuti atikhululukire ife machimo athu, ndi kutipatsa zonse zomwe tikufunikira paulendo wathu.

Atate Wakumwamba, tikuyamikira nthawi ino, nthawi inaso yosonkhana pamodzi, mbali ino ya Umuyaya. Ndipo ife tikuyang’anira m’mawa uno kuti mphamvu zatsopano zichokere kwa Inu, kutipatsa kulimba mtima paulendo womwe uli patsogolo. Ife tasonkhana monga momwe ana Achiheberi adachitira m’mawa kwambiri, kuti titenge mana omwe adaperekedwa kwa iwo usiku wonse, kuti awathandize tsiku lotsatira. Ife tasonkhana kuti tidye Mana a uzimu, m’mawa uno, kutipatsa mphamvu paulendo.

Tiyeni tonse tiyambe pa nthawi ya 6:00 PM. pa nthawi yanu yapafupi kuti mumve Mgonero 62-0204, kenako mneneriyo adzatitengera ku Utumiki wathu wapadera wa Mgonero ndi Kutsukana Mapazi ku m’maliziro a tepiyo, yomwe idzaseweredwa pa pulogalamu ya Lifeline (mu Chingerezi), kapena mutha kupanga dawunilodi utumikiwu mu Chingerezi kapena mu zilankhulo zina podina ulalo womwe uli pansipa.

LACHISANU

Tiyeni ife tipite ku pemphero ndi mabanja athu nthawi ya 9:00 AM, ndipo kenako nthawi ya 12:00 PM, kupempha Ambuye kuti akhale nafe ndikudzaza nyumba zathu ndi Mzimu Woyera pamene tikudzipereka ife eni kwa Iye.

Malingaliro athu abwerere m’mbuyo ku tsiku lija ku Kalvari, zaka zoposa 2000 zapitazo, ndikuwona Mpulumutsi wathu atapachikidwa pamtanda. Tiyeni tikumbukire mtengo waukulu umene Iye analipira chifukwa cha ife. Iye anali Mwana wa Mulungu wopanda uchimo, koma anayenera kuvutika monga momwe panalibe munthu wina aliyense akanavutikira, chifukwa machimo athu anaikidwa pa Iye.

Iye anayenera kumutumiza ku gehena wolangidwa (Mukuona?), chifukwa Iye ananyamula machimo athu. Ndipo Khristu anafa, osati wolungama; Khristu anafa wochimwa. Mukuona? Khristu sanachimwepo Iye mwini, koma Iye ananyamula machimo athu pa Iye.

Kenako pa 12:30 PM, tiyeni tilumikizane pamodzi m’nyumba zathu ndikunva 57- 0419 Ungwiro.

Kenako tiyeni tilumikizane pamodzi m’pemphero mwachangu nthawi yomweyo pambuyo pa utumiki, pokumbukira kupachikidwa kwa Ambuye wathu.

LOWERUKA

Tiyeni tonse tibwere pamodzi mu pemphero nthawi ya 9:00 AM ndi 12:00 PM, ndikukonzekeretsa mitima yathu zinthu zazikulu zomwe Iye adzatichitira pakati pathu.

Ine ndikumva Iye akunena kuti, “Satana, bwera kuno!” Iye ndiye Bwana tsopano. Akufikira, akutenga kiyi ya imfa ndi gehena m’mbali mwake, naipachika pambali Pa Iye Mwini. “Ine ndikufuna nditumikire kukudziwitsani inu. Mwakhala wonyenga kwa nthawi yayitali. Ine ndine Mwana wa Mulungu wamoyo wobadwa kwa namwali. Magazi anga akadali onyowa pamtanda, ndipo ngongole yonse yathunthu yalipidwa! Iwe Siwulinso ndi ufulu mkomwe. Iwe wavulazidwa. Ndipatse ine makiyi amenewo!”

Kenako nthawi ya 12:30 PM, tonse tidzasonkhana pamodzi kuti timve Mawu: 57-0420 Kuikidwa M’manda.

Ndi tsiku la KALATA YOFIWIRA kwambiri bwanji yomwe iyo ili kwa Mkwatibwi Wake padziko lonse lapansi.

Ndiye tiyeni tigwirizanenso pamodzi mu pemphero nthawi yomweyo utatha utumiki.

LAMULUNGU

Tiyeni tidzuke kaye m’mawa monga momwe M’bale Branham adachitira m’mawa pamene bwenzi lake laling’ono, phwiti, adamudzutsa iye nthawi ya 5:00 AM. Tiyeni ife tingoyamika Ambuye chifukwa choukitsa Yesu kwa akufa:

Masiku asanu m’mawa uno, bwenzi langa laling’ono lofiira linaulukira pawindo ndipo linandidzutsa ine. Zikuoneka kuti mtima wake waung’ono unaphulika, ndikunena, “Iye Wauka.”

Nthawi ya 9:00 AM tiyeni tigwirizanenso mu Tcheni chathu cha pemphero, kupemphererana wina ndi mnzake ndikukonzekera kumva Liwu la Mulungu.

Nthawi ya 9:30 AM, Ife tidzasonkhana pamodzi kuti timve Uthenga wathu wa Isitala: 65-0418M Ndi Kutuluka kwa Dzuwa.

Nthawi ya 12:00 PM tidzakweza mawu athu kwa Iye kumuyamika chifukwa cha Mphamvu Yofulumizitsa.

Nthawi ya 3:00 PM, tiyeni tigwirizanenso m’pemphero, kumuyamika chifukwa cha MAPETO A SABATA YODABWISTSA YOMWE IYE WATIPATSA IFE NDI IYE NDI MKWATIBWI WAKE KUZUNGULIRA DZIKO LONSE LA PANSI.

Kwa abale ndi alongo anga akunja, monga chaka chatha, ine ndikufuna kukuitanani kuti mugwirizane nafe pa nthawi ya ku Jeffersonville, nthawi zonse zamapemphero pa ndondomekoyi. Ine ndikuzindikira, komabe, kuti kusewera Matepi Lachinayi, Lachisanu, ndi Loweruka masana pa nthawi ya ku Jeffersonville kungakhale kovuta kwambiri kwa ambiri a inu, choncho chonde musazengereze kusewera Mauthenga amenewo panthawi yomwe ingakhale yoyenera kwa inu. Komabe, ndikufuna kuti tonse tigwirizane Lamlungu nthawi ya 9:30 AM, nthawi ya ku Jeffersonville, kuti timve Uthenga wathu wa Lamlungu pamodzi.

Ndikufunanso kukuitanani inu ndi ana anu kuti mukhale nawo m’mapulojekiti a Creations, kulemba manyuzipepala, ndi maphikidwe, omwe banja lanu lonse lingasangalale nawo limodzi. Tikuganiza kuti mudzawakonda chifukwa onse akuchokera pa MAWU omwe tidzakhala tikuva kumapeto kwa ndondomeko kwa sabata ino.

Zidziwitso pa za kakonzedwe ka mwambo wa mgonero , zinthu zomwe zidzafunike pa mapulojekiti a Creations, ndi zidziwitso zina, onani maulalo omwe ali pansipa.

Tiyeni ife titseke mafoni athu kumapeto kwa sabata ya Isitala kupatula kujambula zithunzi, kumvetsera Zobwereza Za Pa Tsiku, ndikusewera matepi kuchokera ku pulogalamu ya Table, pulogalamu ya Lifeline, kapena ulalo wopangidwa dawunilodi.

Iwo ndi ulemu waukulu kwa ine kukuitanani inu ndi banja lanu kuti mudzabwere pamodzi ndi Mkwatibwi kuzungulira padziko lonse lapansi kumapeto kwa sabata yodzaza ndi KUPEMBEDZA, MATAMANDO NDI MACHIRITSO. Ine ndikukhulupirira kuti ndikwenikweni ndi kumapeto kwa sabata komwe kudzasintha moyo wanu kwamuyaya.

M’bale Joseph Branham