22-1030 Munthu Kuthawa Pamaso Pa Ambuye

Uthenga: 65-0217 Munthu Kuthawa Pamaso Pa Ambuye

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa ana ankhosa a Ambuye,

Momwe mitima yathu imafunira tsiku ili sabata iliyonse pamene tingagwirizane pamodzi kuchokera ku dziko lonse lapansi kuti timve Liwu la Mulungu likulankhula kwa ife Mawu a Moyo yamuyayaya. Palibenso china chimene chimakhutitsa moyo wathu ndi kuthetsa ludzu lathu koma Liwu la Mulungu.

Inu munatiuza ife Atate kuti munda waukulu wokolola wayera, wakupsa, ndipo mbewu zakonzekera nyengo yopunthidwa. Njere tsopano yagona mu Kukhalapo kwa Mwana ndi kucha ku Ufumu wa Mulungu.

Ife tikuyima, Atate, ku kukhudzika kwathu kwa zomwe ife tikuzidziwa kuti ndi Choonadi; Liwu Lanu la pa tepi ndilo Liwu LOKHA limene lingatifikitse ife angwiro, Mkwatibwi Wanu.

Zimakhala zovuta popeza abale ndi alongo athu samatimvetsetsa. Ife tikupempha ndi kuwachonderera iwo kuti asathawe kuchoka pa Kukhalapo Kwake, koma kuti athamangire mu Kukhalapo Kwake.

Ife tikudziwa kuti alipo amuna ambiri odzozedwa omwe Inu munawasankha ndi kuwaika kuti ayang’ane pa zoweta Zanu, amene amakonda Uthenga uwu ndi mitima yawo yonse, koma Atate, iwo akulephera kuyika Liwu Lanu lotsimikiziridwa pa tepi pamaso pawo. Iwo amalephera kuwauza iwo kuti uwu ndi Uthenga wa munthu mmodzi ndi kuti Inu munasankha mwamuna kuti atsogolere Mkwatibwi Wanu. Iwo amalephera kuwauza iwo kuti Liwu Lanu ndilo Liwu LOKHA limene lidzagwirizanitsa ndi kupangitsa Mkwatibwi Wanu kukhala wangwiro.
Ndiyenera “kufuula motsutsa izo.” Lirani motsutsa chirichonse, ndi aliyense, yemwe akutsutsa kusewera Matepi Anu mu mipingo yawo. Lirani motsutsa ntchito yawo, lirani motsutsa mpingo wawo, lirani motsutsa aneneri awo, lirani motsutsa atumiki awo, lirani motsutsa ansembe awo. Ndiyenera kulira motsutsa chinthu chonsecho!

“Ndinene, ndabwera kuti tidzakumane nanu. Mukudziwa, ndikukhulupirira ndikuwuzani zomwe ndichita. Ndili ndi kachinthu kakang’ono pano komwe ndikukhulupirira kuti ndikhoza kupangitsa kuti…kutibweretsere tonse pamodzi, ndi kuchita izi, izo, kapena zina.”

Ine ndiyenera kufuula motsutsa izo, monga Mawu Anu okha, olankhulidwa ndi mneneri Wanu, angatibweretsere IFE PAMODZI.
Kodi kulalikira kwawo kungatheke bwanji? Iwo onse amatsutsana wina ndi mzake ndipo amawona zinthu mosiyana kwa wina ndi mzake, kupatula chinthu chimodzi, iwo onse amavomereza pa^OSATI KUSEWERA MATEPI MMIPINGO YAWO. Zingatheke bwanji zimenezo, Atate?

Inu munatiuza ife kuti ife tiyenera kukhala ndi Mtheradi UMODZI, umene uli Mawu Anu. Inu munatiuza ife kuti Mawu Anu amadza kwa mneneri Wanu, YEKHA. Munatiuza ife kuti iye ndiye YEKHA amene angakhoze kutanthauzira Mawu Anu. Inu munatiuza ife kuti mtumiki aliyense, membala wamba aliyense, munthu aliyense, ANGANE ZOKHA ZIMENE ANANENA. Liwu Lake ndi MAWU OKHA OKHA amene amatsimikiziridwa ndi Lawi Lanu la Moto kuti likhale PAKUTI ATERO AMBUYE.

Sindikunena kuti ndi zabodza kapena sayenera kulalikira. Kapena sindikunena kuti Ambuye sali nawo, kapena iwo sanadzozedwe ndi kuitanidwa kuti azilalikira, koma ndiyenera kulira motsutsa iwo pamene iwo sadzawauza anthu awo kuti kumvetsera matepi ndicho chinthu chofunika kwambiri chimene iwo angachite.

Kusintha joti limodzi kapena kachidutswa kamodzi ndi imfa. Mwapereka njira kwa Mkwatibwi Wanu kuti amve Atero Yehova ndi makutu awo. Kodi angalephere bwanji kulalikira kwa anthu awo kuti ndi Uthenga wofunika kwambiri umene ayenera kumva? Ndi Uthenga wokha umene ine ndingakhoze kunena AMEN kwa Mawu aliwonse, popeza si Mawu a munthu, kapena kutanthauzira kwa munthu kwa Mawu Anu, ndi Mawu Anu Oyera.

Inu munati Uthenga ndi mtumiki ali yemweyo. Mneneri wanu analankhula Izo ndipo Inu mukanazikwaniritsa Izo. Mawu Anu olankhulidwa ndi mneneri Wanu AMAsowa kutanthauzira monga ali Mwana wa Munthu akuyankhula molunjika kwa Mkwatibwi Wake.

Ndiyenera kuwapempha anthu, bwererani ku chikondi chanu choyamba. Bwererani ku chimene inu mukudziwa kuti ndi PAKUTI ATERO AMBUYE. Ngati mwakhala mukuganiza njira yoti mupite kapena choti muchite, bwerani, kukwera nafe sitima usikuuno. Ife tikupita ku Nineve, kukalira. Ife tiri ndi ntchito pamaso pa Mulungu, ndiwo Uthenga uwu wa pa tepi.

Ife tikukhulupirira kuti Kudza kwa Ambuye kwayandikira, ndipo Iye adzakhala ndi Mkwatibwi, ndipo ife tikukonzekera. Ife sitikufuna kalikonse koma Mawu Oyera a Mulungu olankhulidwa ndi mneneri Wake. Tikupita ku Ulemerero, bwerani mudzajowine mu sitima yathu.

Ngati mukukhulupirira kuti Uthenga uwu ndi Choonadi, ndi woyenera kukhalira moyo, wofunika kuufera, bwerani mudzabwere nafe Lamlungu lino nthawi ya 12:00 p.m., nthawi ya Jeffersonville, pamene tikumva Uthenga umene tikukhulupirira kuti ndi wofunikira komanso wachangu kwa ife kuti tiumve: Munthu. Kuthamanga Kuchokera Pamaso Pa Ambuye 65-0217.

Ndinu ana ankhosa anga. Zili bwanji? Inu ndinu ana ankhosa a Yehova amene wandilola kuti ndidyetse.

Bro. Joseph Branham.

Malemba oti muwerenge

Yona 1:1-3
Malaki 4
Yohane 14:12
Luka 17:30