Uthenga: 65-0718M Kuyesa Kuti Umuchitire Mulungu Ntchito Mopanda Kukhala Chifuniro Cha Mulungu
- 26-0426 Kuyesa Kuti Umuchitire Mulungu Ntchito Mopanda Kukhala Chifuniro Cha Mulungu
- 24-0721 Kuyesa Kuti Umuchitire Mulungu Ntchito Mopanda Kukhala Chifuniro Cha Mulungu
- 23-0101 Kuyesa Kuti Umuchitire Mulungu Ntchito Mopanda Kukhala Chifuniro Cha Mulungu
- 21-0509 Kuyesa Kuti Umuchitire Mulungu Ntchito Mopanda Kukhala Chifuniro Cha Mulungu
Wokondedwa Mkwatibwi Wosamalidwa,
Ola lachedwa. Nthawi yafika. Chisankho chiyenera kupangidwa. Mulungu akuchenjeza ana Ake. Ambuye Mulungu wathu walengeza ndi kutsimikizira kwa ife chomwe Choonadi Chake chili ndi Mawu Ake, ndi Mzimu Wake. Osati ndi mphamvu, osati ndi nkhondo, koma ndi Mzimu Wanga, ndipo Mawu Anu ndi Choonadi.
Iye watsimikizira kwathunthu kwa Mkwatibwi lero kuti Yesu Khristu ali yemweyo dzulo, lero, ndi nthawi zonse.Iye watiwonetsa ndi kutiwululira kuti Uthenga ndi mthenga wa ora ali ofanana. Iye wativumbulutsira zinsinsi Zake zonse zomwe zinali zobisika mu Mawu. Iye watitsimikizira Izi ndi Mzimu Wake Woyera. Palibe funso m’maganizo mwathu, m’mitima kapena m’miyoyo yathu. Mawu Ake pa matepi ndi PAKUTI ATERO AMBUYE KWA MKWATIBWI WAKE.
Mulungu nthawi zonse walola njira zambiri kubwera kwa Iye.Iye amapanga chifuniro Chake chongololera kukhala chifuniro Chake Changwiro. Iye mongaso nthawi zonse wapereka CHIFUNIRO CHANGWIRO NDI NJIRA YABWINO KWA ANA AKE. Ambiri amayesa kubwera mwanjira yosiyana pochitira Mulungu ntchito popanda kukhala chifuniro Chake changwiro.Izo Zingawonekere ndikumveka ngati chifuniro Chake changwiro, koma izo sizili monga ndi Mawu Ake.
Ngakhale munthu wamkulu, wodzozedwa kumene, wochokera ku Kukhalapo kwa Mulungu, adapeza vumbulutso loti achite china chake kwa Mulungu, ndipo amafuna kuchichitira Mulungu; koma vumbulutso lomwe anali nalo linali lolakwika.
Aliyense wa ife ayenera kupeza njira Yake yangwiro yoperekedwa. Kodi ife tingadziwe bwanji kuti tili mu chifuniro Chake changwiro ngati wina wodzozedwadi, wochokera ku kukhalapo kwa Mulungu, ndi vumbulutso, si ali mu chifuniro changwiro cha Mulungu?
Pali NJIRA IMODZI YOKHA YODZIWIRA YA CHOWONADI, ndipo Mulungu wapereka njira imeneyo kwa Mkwatibwi Wake.
Liwu la Mulungu Mwiniwake lawuza mpingo uno, ndi inu nonse anthu omwe muli pa matepi, ndi anthu omwe ali olumikizidwa pa intaneti m’madera ena a dziko lapansi, nthawi imeneyo ndi TSOPANO. Iye anatiuza ife kuti timvere mwatcheru Kwambiri zomwe iye anali kunena , ndipo kuti ife TISALEPHERE.
Chotero ine ndikunena, mu Dzina la Yesu Khristu! Musati inu muwonjezere kanthu kamodzi. Musati mutenge, kuyika malingaliro anu omwe mwa Iwo. Inu muzingonena chimene chikunenedwa pa matepi awo. Inu muzingochita chimodzimodzi chimene Ambuye Mulungu wakulamulirani kuti muchite. Musati muwonjezere kwa Iwo.
Iye sananene kuti, ndipo izo sizikutanthauza kuti alaliki sangalalikire Mawu, aphunzitsi sangaphunzitse Mawu, kapena abusa kapena aneneri ife tichite zomwe tayitanidwira kuchita; iwo ayenera, ine ndiyenera.Ife tayitanidwa ndi kudzozedwa kuti tichite zimenezo.Ife tiyenera kuloza ndi kubwereza Uthenga uwu ndi mthenga kwa anthu, chifukwa iwo ndiwo Mawu a tsiku lathu.
Koma Iye akutiuza momveka bwino kuti tonsefe a ife tikhoza kudzozedwa, ndi kudzozedwa kolondola, kudzazidwa ndi Mzimu Wake Woyera, ndi vumbulutso latsopano, ndikukhala kunja Kwa chifuniro Chake. Mu tsiku lathu lino, Iye wapereka NJIRA YANGWIRO yodziwira motsimikiza kuti mukumva Liwu la Mulungu, lochokera kwa Mulungu Mwiniwake. Ndiyo njira YOKHAYO yangwiro.
Utumiki suyenera kungotchula mobwereza kokha ndi kulalikira Uthenga uwu, koma ife tiyenera kusewera Liwu la Mulungu pa matepi kwa anthu. Palibe KUDZOZA KWAKUKULU kuposa kumva Liwu la Mulungu. Palibe njira ina yodziwira popanda mthuzi wa kukayikira kuti zomwe ife tikumva ndi NDIZOMWEZODI zomwe Mulungu ananena.
Mu tsiku lino, mosiyana ndi tsiku lina lililonse mu mbiri ya dziko lapansi, Mulungu wapereka njira yomwe imapangitsa kuti zikhale zosatheka kuphonya izo, ngati inu ndinu Mkwatibwi Wake Wokonzedweratu.Iyo yatsimikiziridwa ndi kuwululidwa ndi Lawi la Moto Mwiniwake kuti ndi Liwu la Mulungu Mwiniwake likulankhula mwachindunji ku Mpingo Wake.
Kwa zaka zikwizikwi, ana a Mulungu akhala akulakalaka ndikukhala nayo njala yakumva Liwu la Mulungu pa Iwo eni.Momwe iwo bwanji anakhumba akanakhalapo tsiku limene lija pamene Yesu analalikira kwa zikwizikwi paphiri. Kumva momwe Iye analankhulira Mawu Ake mwachikondi ndi chifundo. Kumva momwe Iye anayikila kutsimikiza pa Mawu aliwonse. Momwe Iye analankhulira ndi kulimbikitsa mitima yawo.
Ife tili amoyo tsopano ndipo tili mu mkupezeka kwa Mulungu kumva Liwu la Mulungu.
Tsiku lina posachedwa sitidzabwerera ku moyo wamtundu uwu kachiwiri. Tidzabwerera ngati munthu wosafa. Uchimo udzachotsedwa. Satana adzamangidwa kwa zaka chikwi ndipo tidzakhala padziko lapansi lino lomwe Ambuye Mulungu wathu watipatsa.
Ife ndife athunthu handiredi peresenti. Ife sitidakhalepo osangalala kapena mochuluka osakhalapo ndi mafunso m’miyoyo yathu. Ife ndife mmodzi ndi Iye ndi Mawu Ake. Ife ndife Mawu Ake. IFE TILI MU CHIFUNIRO CHAKE CHANGWIRO MWAKUKHALABE NDI LIWU LAKE, MAWU AKE. Iye adzabweranso tsiku lina lililonse tsopano kuti adzatitenge ife limodzi naye.
Zikomo inu Ambuye Yesu!
Ambuye Mulungu wanu wawonetsera kwa inu chomwe chiri Choonadi. Ambuye Mulungu wanu watsimikizira chomwe chiri Choonadi, mwa Mawu Ake ndi mwa Mzimu Wake. “Si mwa mphamvu, si mwa nkhondo, koma mwa Mzimu Wanga.” Ndipo, Mzimu, “Mulungu akufuna iwo amene ampembedza Iye mu Mzimu ndi Choonadi.” “Mawu Anu ali Choonadi.” Ndipo Iye watsimikizira mwathunthu kuti Yesu Khristu ali yemweyo dzulo, lero, ndi nthawizonse. Iye wawonetsera Mbewu ya madzulo kwa inu. Iye wawululira Iyo kwa inu, mu Mawu. Iye wayitsimikizira Iyo kwa inu, mwa Mzimu Wake.
Ndi mtima wanga wonse ine ndikukuitanani aliyense wa inu kuti mubwere kudzalumikana ndi gawo la Mkwatibwi Wake pamene tikulumikizana kuchokera padziko lonse lapansi nthawi ya 12:00 PM, nthawi ya ku Jeffersonville, kuti tidzamve Liwu Lake likulankhula kudzera mwa mthenga wake wachisanu ndi chiwiri wa mngelo ndikutibweretsera ife Uthenga: Kuyesa Kuti Umuchitire Mulungu Ntchito Mopanda Kukhala Chifuniro cha Mulungu 65-0718M.
M’bale Joseph Branham
Malemba Owerenga Musanamve Uthenga:
Deuteronomo 4:1-4 / 4:25-26
1 Mbiri 13
1 Mbiri 15:15
Masalimo 22
Mariko Woyera 7:7
Yoweli 2:28
Amosi 3:7
Malaki 3
Mateyu Woyera 11:1-15
1 Akorinto 13:1