Uthenga: 65-0429E Kusankha Kwa Mkwatibwi
Wokondedwa Mkwatibwi Wosankhidwa,
Pamene ife tikumvetsera Uthenga uwu, Kusankha Kwa Mkwatibwi, ena amaganiza kuti mneneri akungolankhula ndi kutilangiza za khalidwe ndi thunthu limene mwamuna ayenera kuyang’ana akamasankha mkazi amene akufuna kukhala mkazi wake. Izo ndi zoona, iye akutero, koma pali kalata yeniyeni yobisika yachikondi m’Mawu Ake. Zimene Iye akuulula kwa Mkwatibwi Wake ndi zozama kwambiri. Mulungu akulankhula ndi iye mwachindunji, kumuuza zomwe ankafuna mwa Iye, ndi chifukwa chake Iye anamusankha iye kuchokera pachiyambi. Iye anafuna kuti Iye adziwe kuti wamusankha iye kukhala MKWATIBWI WAKE WOKONDEDWA WOKOMA MTIMA yemwe Iye ankafuna kugawana naye Umuyaya Wake.
Pachiyambi, Mulungu anali kufunafuna Mkwatibwi amene adzakhala ndi Khalidwe Lake lomwelo. Mzimu Wake womwewo ukanadzaonekera mwa Iye. Iye anafuna Mkwatibwi amene akanadzakhala wodzipereka kwambiri kwa Iye, ndi Mawu Ake olonjezedwa,Kufikira mpaka Maganizo omwe anali mwa Iye adzakhale mwa Iye. Iye ayenera kuumbidwa monga momwe Iye alili.
Iye anafuna kuti Iye akhale thupi Lake lomwelo, mafupa omwewo, Mzimu womwewo, chilichonse chomwecho, basi chimodzimodzi monga Iye. Awiriwa a iwo adzakhala M’MODZI.
Iye sakanakhala wa chimasomaso mmaso mwake . Iye sakananyengereredwa ndi ma liwu ena aliwonse. Iye akanakhala woona mtima komanso wokhulupirika kwa Iye, mosasamala kanthu za zomwe wina anganene. Iye akanamutenga Iye pa Mawu Ake. Chilichonse chimene Iye adanena, AKANAKHULUPIlIRA MAWU ONSE, zilibe kanthu kaya ndi motalika bwanji zingatenge kuti zikwaniritsidwe, iye Akanakhulupirira izo. Iye akanakhalabe ndi Mawu Ake.
Iye akanakonda Iye, ndipo Iye yekhayo. Iye sanafunikire kumupatsa iye chuma chambiri, iye anali ndi Ngale yamtengo wapatali, Vumbulutso lenileni la Iye. Iye akanadziwa, iwo anali M’MODZI ndipo ndi ofanana. Mzimu Wake ukanakhala mwa Iye. Chilichonse chimene Iye akanafuna, Iye akanamupatsa Iye; chomwe Iye ankayenera kuchita chinali kupempha ndi kukhulupirira, ndipo Iye akanachita icho.
Iye ankadziwa kuti Iye akanapita kwa nthawi yaitali kuti akamumangire nyumba yomwe ikanakhala ndi chilichonse chofanana ndi Iye. Iye ankayimanga iyo momwe Iye akanakondera. Iye ankadziwa tsiku lina Iye adzabweranso kwa Iye, monga momwe Iye analonjezera, ndiye kuti adzakhala ndi Mgonero Waukwati waukulu kwa zaka chikwi. Kenako, adzapita limodzi ku Nyumba yokongola imene Iye adamumangira iye kuti akhale Kwamuyaya.
Palibe china chilichonse chomwe chingakhale chovuta kwa Iye. Iye Sadzafuna china chilichonse. Iye adzakhala choncho wokhutira ndi wokhutsidwa ndi pokhala ndi Vumbulutso podziwa yemwe Iye ali, ndi kuti Iye ndi ndani. Iye anadziwa kuti Iye adzasunga Mawu Ake. IYE ADZAKWANIRITSIDWA, PODZIWA KUTI IYE NDIYE YOMWE IYE ANASANKHA KUTI AKHALE MKWATIBWI WAKE.
Abale ndi alongo anga, Mulungu wamphamvu wa Kumwamba ndi dziko lapansi anayang’ana kupitilira mumuyaya ndipo WAKUSANKHANI… INU KUKHALA MKWATIBWI WAKE WOSANKHIDWA WOKOMA MTIMA.
Ine ndikukuitanani inu kuti mubwere mudzalumikizane nane limodzi ndi gawo la Mkwatibwi Wake Lamlungu lino, pamene Iye akulankhula kudzera mwa mngelo wake wamphamvu ndikutiuza kuti ndife Mkwatibwi Wake Wosankhidwa.
M’bale Joseph Branham
Uthenga: 65-0429E Kusankha Kwa Mkwatibwi
Nthawi: 12:00 P.M. Nthawi ya ku Jeffersonville
Malemba:
Genesis 24:12-14
Yesaya 53:2
Chivumbulutso 21:9