Uthenga: 61-0806 Sabata La Makumi Asanu Ndi Chiwiri La Daniele
- 25-0216 Sabata La Makumi Asanu Ndi Chiwiri La Daniele
- 16-1126 Sabata La Makumi Asanu Ndi Chiwiri La Daniele
Okondedwa Iwo Akuyang’anira Ndinso Akuyembekenzera,
Pali chisangalalo pakati pa Mkwatibwi kuposa kale. Tili pa kuyembekezera kwakukulu; Chaka chathu chachisangalalo chikukonzekera kuti chichitike. Mkwatibwi wayembekezera motalika kwambiri kuti tsiku ili lifike. Mapeto a nyengo ya m’badwo wa Amitundu yafika ndipo chiyambi cha muyaya ndi Ambuye wathu chiyamba posachedwapa.
Ife tikumvetsa nthawi yomwe tikukhalamo pa kumva Mawu. Nthawi yatha. Nthawi ya Mkwatulo yayandikira. Tafika. Mzimu Woyera wabwera ndi kuwulula kwa Mkwatibwi Wake zinthu zonse zazikulu, zakuya, zinthu za zinsisi.
Ife tiri mu kusimidwa, kufunafuna Mulungu; kudzikonzekeretsa tokha. Tataya zinthu zonse za dziko lino. Zosamalira za moyo uno sizitanthauza kanthu kwa ife. Chikhulupiriro chathu chafika patali kwambiri kuposa kale lonse. Mzimu Woyera ukumupatsa Dona Wake wosankhidwa Chikhulupiriro chokwatulitsa, kotero Iye akhoze kubwera ndi kumuchotsa Iye.
191 Masabata sikisite naini awa analondolera mwangwiro; kupita kwina kwa Ayuda kumalondolera mwangwiro; m’badwo wa mpingo umalondolera mwangwiro. Ife tiri pa mapeto a nthawi, nthawi yotsiriza, m’badwo wa mpingo wa Laodikaya, kutha kwa iwo. Atumiki nyenyezi onse alalikira uthenga wawo. Iwo wapita kunja. Ife tikungogubuduka.
Ndi nthawi yodabwitsa bwanji yomwe Ife tikukhalamo. Ndi nthawi yovuta kwambiri pamene m’dani akulimbana ndi aliyense kuposa kale. Iye akuponya zonse zimene ali nazo kwa ife. Iye ali mu kusimidwa, chifukwa akudziwa kuti nthawi yake yafika kumapeto.
Koma panthawi yomweyomweyo, Ife sitinakhalepo osangalala kwambiri mmiyoyo yathu.
• Sitinakhalepo pafupi ndi Ambuye.
• Mzimu Woyera amadzaza mum’tsempha uliwonse wa thupi lathu.
• Chikondi chathu pa Mau ake sichinakhale chokulirapo.
• Vumbulutso lathu la Mau ake limadzaza moyo wathu.
• Tikugonjetsa mdani aliyense ndi Mau.
NDIPO, sitinakhalepo otsimikiza kwambiri kuti ndife ndani:
• OKONZEDWERATU
• OSANKHIDWA
• OSANKHIDWA
• Mbewu Yachifumu
• OKOMA APA MTIMA
• AMUYAYA, IWO OVALA MWINJIRO WOYERA, MAYI JÉZU, OMVETSERA KU MATEPI, OWUNIKILIKIDWA, NAMWALI WOLANGIDWA, WODZAZIDWA NDI MZIMU, WOSAGONJETSEDWA, WOKHAZIKITSIDWA KWAUZIMU, WOSAIPITSIDWA, MKWATIBWI WA MAWU NAMWALI.
Mchiyani Chikubwera chotsatira ? Mwala ukubwera. Tikuyang’ana, kuyembekenzera ndi kupemphera mphindi iliyonse tsiku lililonse. Palibenso china chilichonse chovuta koma kudzikonzekeretsa tokha pa kubwera kwake.
Sikuti, “Tikuyembekeza choncho”, TIKUDZIWA. Kulibenso zokaikitsa zochuruka zina zilizonse. Mu M’kamphindi, m’kuthwanima kwa diso kudzakhala kuti kwatha, ndipo tidzakhala kuti tili kumbali inayo ndi okondedwa athu onse ndi IYE pa Mgonero wathu wa Ukwati.
NDIPO ICHO NDI CHIYAMBI CHABE …NDIPO KULIBE MAPETO!!
Bwerani mudzakonzekere Mgonero wa Chikwati uwu nafe Lamlungu lino pa 12:00 P.M., nthawi ya ku Jeffersonville, pamene Mulungu akuyankhula kupyolera mwa mngelo Wake wamphamvu, yemwe Iye anamutuma kuti adzatsogolere Mkwatibwi Wake, monga iye akuuzira, ndi kuwulula, zinsinsi zonse za Mulungu.
M’bale. Joseph Branham
Uthenga: 61-0806 – Sabata La Makumi Asanu Ndi Awiri La Daniele