Category Archives: Uncategorized

26-0628 Fyuluta Ya Munthu Woganiza

Uthenga: 65-0822E Fyuluta Ya Munthu Woganiza

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mkwatibwi wa Khristu,

Tiyeni tibwere pamodzi Lamlungu pa 12:00 PM, nthawi ya ku Jeffersonville, kuti tidzamve 65-0822E Fyuluta Ya Munthu Woganiza.

M’bale Joseph Branham

26-0621 Khristu Akuwululidwa Mu Mawu Ake Omwe

Uthenga: 65-0822M Khristu Akuwululidwa Mu Mawu Ake Omwe

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa mfumukazi

Ndipo Mkwatibwi lero ndi wotengedwa kuchokera ku thupi la Khristu, amene ali kuchita ndi kupanga basi ndendende monga Iye anati Iye akanati adzachite kwa tsiku lino, Mkwatibwi, Mfumukazi; Mfumu ndi Mfumukazi.

Pamene Yesu anakhala Mawu onsewo, ndiye kuti tinali gawo la Iye KALE. Palibe mdierekezi, palibe mphamvu, palibe chomwe chingatichotsere zimenezo.Chimenecho ndicho chimango cha moyo.

Ndi chitsitsimutso chotani chomwe Mkwatibwi akukhala nacho ndi Uthenga uliwonse womwe ife tikumva. Izo ndi zopitilira mawu aumunthu ku fotokoza. Palibe mthunzi uliwonse wa kukayika, Mulungu watisankha ife ndipo watipatsa ife Vumbulutso LENI LENI la Mawu Ake a lero. Chifukwa chake, tikudziwa kuti ndife ndani, Mfumukazi Yake.

Liwu la Mulungu likulankhula ndi Mkwatibwi Wake pa matepi likumupanga kukhala wangwiro Mkwatibwi Wake. Palibe utumiki wina, palibe liwu lina; palibe chomwe chingapange kukhala wangwiro Mkwatibwi Wake koma Mulungu Mwiniwake akulankhula kudzera m’milomo ya munthu mwachindunji kwa Mkwatibwi Wake. Ena angafune cholowa m’malo, koma Mkwatibwi Wake sadzakhutira ndi china chilichonse koma LIWU Lake, kalata Yake yachikondi kwa Mkwatibwi Wake; chifukwa Nkhosa Zake zimangofuna kumva liwu Lake.

Anthu amati timaika kutsimikizira kwambiri pa mneneri. Izo zili choncho za chilendo kuti anthu savomereza kuti Atate Wamkulu Wakumwamba Mwiniwake anasamala kwambiri mngelo Wake kotero kuti anaika kufunika kwakukulu pa chilichonse chokhudza iye; momwe ankavalira, momwe ankachitira zinthu, khalidwe lake, machitidwe ake.

Anamuvekanso zovala zomwe ankavala; chibadwa chake, cholinga chake, chilichonse momwe ankayenera kukhalira, anasankhidwa mwangwiro ndi Mulungu Mwiniwake chifukwa cha ife…ndiyeno mkumati ife timaika kutsimikizira kwambiri pa mneneri.

Kwa ife, Liwu lomwe lili pa matepi si liwu la munthu, komanso sililankhulidwa ndi munthu, kubweretsedwa ndi munthu, kapena silingavumbulutsidwe ndi munthu. Ndi Liwu la Mulungu lomwe lawululidwa ndi Mulungu Mwiniwake, Wotanthauzira Wake, Khristu akudziwulula Yekha mu Mawu Ake.

Ena amatha kumva, koma sazindikira mokwanira. Inu mutha kuwauza, kuwawonetsa, koma Iwo mophweka sangathe kuwona. Ife timawakonda, kuwapempherera, koma zomwe Mulungu watiwululira ndi Ungwiro Wake.

Pano Pali choyesera cha Litimasi pa kugawikana kwakukulu pakati pa Mkwatibwi wa Khristu lero omwe iwo amati ali ndi Vumbulutso lowona la Uthenga waukulu uwu wa nthawi yotsiriza.

Tanthauzo la choyesera cha Litimasi: Chimodzi, fundo yotsimikizika, funso, kapena chochitika chomwe chimawulula mwachangu mtundu weniweni, maonekedwe, kapena udindo wa chinthu china (kapena winawake).

Ndiloleni ine ndinene kaye izo mobwereza, ndimakhulupirira mu utumiki weniweni woyitanidwa ndi Mulungu. Pali kufunika, ndi malo, pa udindo uliwonse. Lemba limati utumiki wa amuna awa ndi wopangitsa oyera mtima kukhala angwiro, koma silinena kuti utumiki uliwonse wofutukuka pasanu udzapangitsa oyera mtima kukhala angwiro. M’bale Branham amatiuza momveka bwino kuti utumiki mu m’badwo uliwonse umasochera, ndiye kodi IWO angapange bwanji Mkwatibwi kukhala wangwiro?

Pali Iwo ambiri, alaliki ambiri, aphunzitsi, atumwi ndi aneneri omwe alalikira kuti amakhulupirira Uthenga wa nthawi yotsiriza uwu ndipo kuti M’bale Branham anali Liwu la Chivumbulutso 10:7, omwe tsopano iwo akunena kuti ndi zabodza, iye ndi wonyenga, ife ndife a mwano.

Awa anali atumiki olemekezeka kwambiri okhala ndi mipingo yayikulu omwe adayenda padziko lonse lapansi ndikutumikira. Amaonedwa ngati atsogoleri akuluakuku mu utumiki wofutukuka pasanu, akulalikira m’misonkhano ndi m’matchalitchi ku United States konse. Iwo anali ndi utumiki waukulu pamaso pa anthu, ndipo anawatsatira ndikuwakhulupirira kuti anali amuna akuluakulu a Mulungu.

Ndiye pali atumiki masiku ano omwe amadziwika kwambiri ngati atumiki enieni awutumiki wofutukuka pasanu omwe amati akukhulupirira Uthengawu mwa kutchula mobwereza ndi kuulalikira iwo, koma iwo amanenanso kuti Uthenga uwu si uli Mtheradi. Masiku a Uthenga wa munthu mmodzi anatha. Utumiki wofutuka pasanu tsopano ndiwomwe woti umupange Mkwatibwi kukhala wangwiro, ndipo ndikolakwika kusewera matepi mu tchalitchi, kubwereza mawu ochepa.

Tikudziwa kuti padzakhala odzozedwa abodza mu nthawi yotsiriza; mneneri anatichenjeza kuti tichenjere nawo. Utumiki wawo udzakhala odzoza. Iwo adzakhala ndi Mzimu Woyera, motero iwo azizatchula mobwereza Uthenga wa ola lino. Adzakhala PAFUPI KWAMBIRI moti iwo akanadzanyenga osankhidwa omwe ngati n’kotheka.

Izo si zipembedzo zimenezo. Iwo sanayambe anyengapo osankhidwa. Chifukwa chake, ziyenera kukhala pafupi kwambiri kuposa pamenepo. Izi sizikutanthauza kuti mtumiki ALIYENSE wasochera, osati mwanjira iliyose ayi. Pali amuna akuluakulu a Mulungu omwe amalalikira ndi kuphunzitsa choonadi, koma pali chinthu china chomwe wokhulupirira aliyense ayenera kuzindikira ndikudzifunsa:

Kodi mtumiki amene mukumutsatira angalakwitse?
Kodi inu munganene kuti ameni ku mawu onse amene iye amalalikira?
Kodi inu mumakhulupirira kuti Mawu aliwonse amene iye amaphunzitsa ndi Pakuti Atero Ambuye?
Kodi liwu lake ndi Liwu lofunikira kwambiri lomwe inu muyenera kumva?
Kodi iye angalalikire chinthu cholakwika?
Kodi iye angalakwitse ngakhale atalalikira Uthenga kwa zaka 30? Kodi iye angalephere?
Kodi iye angakuuzeni zinthu zolakwika?
Kodi iye anganyengedwe?

Tsopano dzifunseni mafunso omwewo okhudza Mawu a Mulungu otsimikiziridwa omwe mungamve pa matepi.

Kodi Uthenga womwe uli pa matepi ungalakwitse: AYI
Kodi inu mungakhulupirire ndi kunena AMENI ku Mawu aliwonse amene iye akunena? INDE
Kodi ilo lingalephere? AYI
Kodi iye angalalikire zinthu zolakwika? AYI
Kodi ilo lingakuuzeni inu chinthu cholakwika? AYI
Kodi inu mungaike malo anu okhazikika pa Mawu onse amene mukumva…INDE!!!
Kodi ilo Ndi Liwu La Mulungu: INDE

N’chifukwa chiyani ine ndikunena zinthu zimezi? Kusonyeza kuti anthu ONSE akhoza, ndipo amachita, kulakwitsa, koma LIWU LA MULUNGU pa matepi silingalakwitse. Ndicho chifukwa chake ndi LIWU LOFUNIKA KWAMBIRI LIMENE INU MUYENERA KUMVA. Ndicho chifukwa chake utumiki uyenera kusewera matepi ku mipingo yawo. Ndi NJIRA YANGWIRO YOPEREKEDWA ndi Mulungu imene wapangira Mkwatibwi Wake.

Ndithudi, ndikukhulupirira kuti inu mungamve ena, koma Liwu lokhalo limene Inu MUYENERA KUMVA ndikukhulupirira Mawu onse ndi Liwu lomwe lili pa matepi. Liwu limenelo ndi LIMODZI LOKHALO limene tinganene AMEN ku Mawu onse.

Ili ndi lamulo la Mulungu, inu muyenera kukhulupirira Mawu onse, ndipo Mawu omwe mumamva pa matepi ndi MAWU OKHAWO amene wotsimikiziridwa ndi Lawi la Moto kuti ndi choonadi. Mulungu anati William Marrion Branham ndiye womasulira waumulungu yekhayo wa Mawu Ake, chifukwa Si mawu ake, Ndi Mawu a Mulungu.

Musasinthe kadontho kamodzi kapena kachidutswa. Palibe munthu amene ali wangwiro moteromo; Liwu la Mulungu lokha ndilo langwiro moteromo. Ngakhale pamene ife sitikumvetsa zomwe tikumva, tiyenera kungokhulupirira kuti ndi Mawu a Mulungu otsimikiziridwa kwa Mkwatibwi Wake.

Zoonadi, Mzimu Woyera ukutsogolera amuna a Mulungu. Zoonadi, Mzimu Woyera wawaitana iwo kuti akhale abusa ndi alaliki ndi aphunzitsi; nzoona, koma si angwiro. Koma Mulungu wapanga njira yoti mumve MAWU ANGWIRO nthawi iliyonse inu mukasonkhana.

Anthu, komanso utumiki, akufuna amlowa mmalo lero. Kodi inu mungaganizire wina kuchita kwa mtumiki zimene Iwo amachitira M’bale Branham?… “Ndikupatsani mphindi sate ndiye inu muyenera kuyima, ndili ndi uthenga womwe ndiyenera kubweretsa.

Inu mukhoza kumva matepi nthawi iliyonse. Ine ndikudziwa zomwe mpingo uwu uyenera kumva zomwe zikuchitika lero.” Ambiri ngakhale sangasewere ngakhale gawo la tepi, ndipo amati n’kulakwa kusewera Liwu la Mulungu m’matchalitchi awo.

Kodi wina aliyense amene ali ndi maganizo abwino angaganize mtumiki amene angapange chifukwa, chifukwa chilichonse, kuti asasewere Liwu la Mulungu m’tchalitchi chawo chifukwa iwo amakhulupirira kuti iwo ayenera kulalikira? Iwo amanena zimenezo, koma iwo sakhulupirira kuti ndi Liwu la Mulungu, kapena iwo sangapereke chifukwa chilichonse choti asasewere matepiwo.

Kodi wina anganene bwanji kuti amakhulupirira kuti ili ndi Liwu la Mulungu ndipo sangafune kulisewerera m’tchalitchi chawo? Kodi anthu amene amanena kuti amakhulupirira kuti ndi Liwu la Mulungu lomwe likulankhula ndipo safuna kuwawuza abusa awo kuti awasewere matepiwo m’matchalitchi awo? Chifukwa ali ndi mzimu womwewo.

Musakhale Nikodemo ndikunena kuti, “Ine ndikuona ndipo ine ndikukhulupirira ilo. Ndi Mwana wa Munthu akudziulula yekha mu thupi la munthu. Ndi Pakuti Atero Ambuye. Ndi Uthenga wangwiro. Ndi Liwu la Mulungu pa matepi, koma ine sindingathe kuchepetsa utumiki wanga ndikunena kuti Liwu limenelo ndilo lofunikira kwambiri kuti mpingo wanga umve.”

Abale ndi alongo, inu simungakhoze kugwirizana nane ndendende kokha pa izi. Ine sindikupempha inu kuti muchite zimenezo. Chinthu chokhacho, inu ingoganizirani izo. Zimene inu mundiuza ine, ine ndidzaziganizira izo. Ngati atumiki alankhula ku mpingo wawo kuti sakhulupirira kusewera matepi m’matchalitchi awo, palibe vuto, m’bale wanga. Inu muwadyetse chilichonse chomwe inu mukufuna.

Ine ndikuyesetsa mwa ubwino wanga kwambiri kuti ndikhale wolondola ndi Mawu, chifukwa nkhosa sizifuna china chilichonse koma chakudya cha nkhosa ndipo ife timakhulupirira kuti Liwu pa Matepi ndi Chakudya chathu cha Nkhosa. Ndicho chimene timakhala nacho moyo: Mawu aliwonse otuluka…Osati Mawu okha tsopano ndi kale; koma Mawu onse otuluka mkamwa mwa Mulungu olankhulidwa pa matepi; ndicho chimene ife timakhala nacho moyo.

Mulungu andikhululukire ine ndipo inu mundikhululukire ine ngati ine ndakukhumudwitsani Inu kapena ndanena china chake cholakwika. Ichi ndi chokhacho chimene ife timakhulupirira ndikuona kuti ndicho Choonadi chomwe ife timakhala nacho moyo. Mulungu watipatsa ife NJIRA YANGWIRO kuti ife timve Liwu Lake ndipo ife timalikonda ilo.

Monga mwachizolowezi, ine ndikuitana aliyense amene akufuna kuti adzalumikizane nafe kudzanva Liwu Limenelo pa nthawi yofanana, kuti adzagwirizane nafe pa 12:00 PM, nthawi ya ku Jeffersonville, komwe tidzagwirizana ngati Gawo Limodzi kumva: 65-0822M Khristu Akuwululidwa Mu Mawu Ake Omwe.

M’bale. Joseph Branham

Malemba Oyenera Kuwerenga Musanamve Uthenga:
Eksodo 4:10-12
Yesaya 53:1-5
Yeremiya 1:4-9
Malaki 4:5
Luka Woyera 17:30
Yohane Woyera 1:1 / 1:14 / 7:1-3 / 14:12 / 15:24 / 16:13
Agalatiya 1:8
2 Timoteo 3:16-17
Ahebri 1:1-3 / 4:12 / 13:8
2 Petro 1:20-21
Chivumbulutso 1:1-3 / 10:1-7 / 22:18-19

26-0614 Ndipo Osadziwa Izo Ayi

Uthenga: 65-0815 Ndipo Osadziwa Izo Ayi

PDF

BranhamTabernacle.org

Okondedwa Iwo Osankhidwa

Kubadwa kwatsopano ndi Khristu, ndi vumbulutso. Mulungu wawululira kwa iwe chinsinsi chachikulu ichi, ndipo kumeneko ndi Kubadwa kwatsopano. Tsopano kodi iwe ungachite chiyani pamene ungalibweretse gulu lonselo pamodzi? kumene vumbulutso likumakhala mwangwiro mu chiyanjano,

Mulungu akusonkhanitsa gulu lake lonse la Mphungu pamodzi mumgwirizano wangwiro akuulula Mawu Ake kwa Mkwatibwi Wake.

Njira ya Mulungu ya kukhala ndi mfumu, monga Davide anali, inali yolondola, ndipo inu mumakhala ndi chimake chimodzi cha lingaliro. Monga mtsogoleri mmodzi ndi gulu la atsekwe, kapena zina zotero, inu simungakhoze kutenga awiri kapena atatu a iwo. Ndiye, inu mukawasokoneza iwo palimodzi, inu mumabwera ndi lingaliro la mtundu uliwonse.

Ndiye ife tiyenera kuchita chiyani, Ambuye?

Chinthu chokha chimene inu muyenera kuchita ndicho kungopangitsa Liwu Langa kudziwika; iwo akulidziwa ilo, pakuti nkhosa Zanga zimadziwa Liwu Langa.”

Kodi Liwu Lanu Langwiro la Lero Ndi Liti, Ambuye?

Ngati ine ndinakukhumudwitsani mwa kunena zimenezo, mundikhululukire, koma, ndinamvelera kuti mwina icho chinazembedwa, koma, Ine ndine Liwu la Mulungu kwa inu.

Ife timakhulupirira zimenezo ndi mtima wathu wonse. Umu ndi momwe ife timamvera, Ambuye

Iwo sasowa kutsimikizira chirichonse mwasayansi, kapena kumufunsa Msaduki aliyense kapena Mfarisi, kapena china chirichonse, za izo. Ine ndinanena izo, iwo akhulupirira izo, pakuti nkhosa Zanga zimamva Liwu Langa.

Kodi Liwu lomwe lili pa matepi kwa Mkwatibwi Wanu ndi lotani?

Ili ndi Liwu la Mulungu mu mawonekedwe a kalata, chifukwa Ili ndi vumbulutso lathunthu la Yesu Khristu, Chipangano Chakale ndi Chatsopano zitayikidwa palimodzi. Ameni. Apo inu muli.

Kodi matepi akadali ofunikirabe lero?

Ine ndikudziwa kuti, ndikadzachoka pa dziko lapansi lino, matepi awo ndi mabuku awo azidzakhalapobe, ndipo ambiri a inu anthu aang’ono mudzapeza, mu masiku akudza, kuti izi ndi chimodzimodzi Choonadi,

Ambuye, ife tikukhulupirira kuti matepi ndi mabuku ndi moyo wanu, utumiki wanu wamoyo womwe munamusiyira Mkwatibwi Wanu.

N’chifukwa chiyani matepi ndi LIWU LOFUNIKA KWAMBIRI kuti ife timve?

Ife tiri mu m’badwo wachinyengo kwambiri umene ife tinakhalamo konse. “Iwo ukananyenga Osankhidwa omwe ngati izo zikanakhala zotheka,” chifukwa iwo ali nako kudzoza, iwo akhoza kuchita chirichonse monga ena onse.

Aliyense amene adzawonjezere mawu amodzi kwa Awa, kapena kutenga Mawu amodzi kwa Iwo.” Iwe uyenera kukhala nawo mtheradi penapake.

Motero, Mtheradi wathu chiyenera kukhala Mawu a Mulungu.Inu mwatiululira kuti Mawu a Mulungu ndi Liwu la Mulungu ndi ofanana. Liwu ndi malingaliro enieni a Mulungu olankhulidwa, monga momwe munachitira ndi aneneri pamene munalemba Baibulo; koma m’masiku otsiriza ano, munasunga Mawu Anu, Liwu lanu, powajambula ndikuwayika pa tepi. Choncho, Liwu Lanu lolankhulidwa pa matepi ndi Mtheradi kwa Mkwatibwi.

Anthu saganiza kuti ndikofunikira kusewera Liwu m’tchalitchi chawo masiku ano. Amaphunzitsidwa m’matchalitchi awo kuti M’bale Branham sananene kuti azisewera matepi m’tchalitchi, iwo amangofuna basi kumva mtumiki wautumiki ndi kungowabwerezera zidutswa za Mawu.

Ndipo ngati mpingo uli mtheradi wanu, inu simumalabadira zimene aliyense anena. Ndiwo mtheradi wanu. O Mulungu, thandizani izi kuti zimire mkati! Kwa ine, chinthu chonse ncholakwika. Mawu a Mulungu ndiwo mtheradi. Chirichonse chimeme Mawu anena, ndiye ndiko kulondola.

Iye anali kuyembekezera kuti iwo amuitanire Iye. Ndicho chimene Iye akuyembekezera usikuuno, kuti inu mumuitanire Iye.
Zindikirani, pamene ophunzira awo anamuitanira Iye umo ku chiyanjano chawo kuzungulira gome,

Kodi wina anganene bwanji, kulungamitsa, kapena kupereka zifukwa, iwo amene akunena kuti iwo akukhulupirira Uthenga wa nthawi yotsiriza, kuti asasewere matepi m’matchalitchi awo pamene ali ndi mwayi womva LIWU LIMENE LA MULUNGU? Ndi Mawu omwe Mulungu analankhula kudzera m’milomo ya munthu kudzera mwa mneneri wake wodzozedwa. LIWU LOKHALO lomwe latsimikiziridwa ndi Lawi la Moto, lotsimikiziridwa mwa kudziwa zinsinsi zomwe za mumtima, lotsimikiziridwa ndi zizindikiro ndi zodabwitsa, kuti NDI Liwu la Mulungu kwa m’badwo uno.

Kodi wina angapange bwanji zifukwa, kufotokozera, kapena kusakhala ndi chilakolako chomva Liwu la Mulungu nthawi iliyonse akasonkhana?

Ambuye, musandilole ine kuti ndisatenge Liwu Lanu pa matepi mwachibwana. Mundilole ine nthawi zonse ndilengeze ku dziko lonse lapansi Ndi Liwu LOKHA lomwe ayenera kumva. Mundilole ndilengeze kwa Mkwatibwi Wanu, CHONSE CHOMWE AKUFUNIKA NDI LIWU LANU PA MATEPI.

Ife timakonda kuyanjana. Timakonda kulankhula za Inu ndi kutchula zidutswa za Mawu Anu, koma palibe china chachikulu chomwe inu mukanachita kwa Mkwatibwi Wanu kuposa kutipatsa Mawu Anu pamwamba pa Mawu, Vumbulutso la Liwu Lanu, kenako kuzindikira YEMWE IFE TILI, MKWATIBWI WANU WOKHULUPIRIKA.

Momwe ine ndingapitirire ndi kupitilira, ndikusonkhana pa vumbulutso lalikulu lomwe Mulungu watipatsa ife. Palibe mapeto; koma chinthu chachikulu chomwe ine ndingachite ndikukuitanani inu kuti mubwere mudzamve nokha Liwu la Mulungu ndi gawo la Mkwatibwi Lamlungu pa 12:00 PM, nthawi ya Jeffersonville, pomwe tidzanva: 65-0815 – Ndipo Osadziwa Izo Ayi.

M’bale Joseph Branham

Malemba oti muwerenge:
Chivumbulutso 3:14-19
Akolose 1:9-20

26-0607 Zochitika Zimamveka Bwino Ndi Uneneri

Uthenga: 65-0801E Zochitika Zimamveka Bwino Ndi Uneneri

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mkwatibwi wa Khristu,

Tiyeni tidzabwere pamodzi Lamlungu pa 12:00 PM, nthawi ya Jeffersonville, kuti tidzamve 65-0801E Zochitika Zimamveka Bwino Ndi Uneneri.

M’bale Joseph Branham

26-0531 Mulungu Wa M’badwo Woipa Uno

Uthenga: 65-0801M Mulungu Wa M’badwo Woipa Uno

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Namwali wamng’ono wa Khristu, Mawu, Gulu la Nkhosa, Mkwatibwi:

Momwe mitima yathu inasangalalira kwambiri titamva mngelo wake wamphamvu akulengeza kuti ndife Mbewu ya Mulungu yokonzedweratu yomwe singachite china chilichonse koma kutsatira Liwu Lake. Izo zimatanthauza zambiri kuposa moyo kwa ife. Inu mukhoza kutenga miyoyo yathu, koma inu simungathe kutenga Liwu Lake. Ife ndife amodzi ndi Mawu Ake. Ife Ndife amodzi ndi Liwu Lake. Ife ndife amodzi ndi Iye.

Izo zikuwoneka zachilendo kwa ife kotero kuti ife sitikumvetsedwa bwino komanso kupangidwa msangulutso chifukwa ife timati timakhulupirira mu nkusewera matepi; kuti ilo ndi Liwu la Mulungu likulankhula ndi Mkwatibwi Wake. Satana ali ndi anthu wanyengedwa kotero iwo amaganiza kuti mwa ife kulengeza kuti ndife mpingo wa tepi, ndi chinthu chinachake chosemphana ndi Mawu, cholakwika, ndipo tikusocheretsedwa, pomwe nthawi zonse Ndi njira yangwiro yoperekedwa ndi Mulungu kwa Mkwatibwi Wake.

Kodi iyo ingakhale njira ina bwanji? Ngati inu mutatanthauzira molakwika Mawu amodzi omwe adalankhulidwa,inu mwatayika.Iwo angakhale ndi chifukwa ndinso cholinga choyenera, koma ndikukhala olakwa. Wina akhoza kudzozedwa ndi Mzimu Woyera koma nkukhalabe wolakwa.

Ngati Mulungu akanakhala kuti sanapereke njira yoti Mkwatibwi Wake amve yekha Mawu onse, ndiye kuti pakanakhala njira ina. Koma Iye wapereka njira kwa munthu aliyense padziko lapansi kuti akhale ndi mwayi womva Mawu akulankhula kwa iwo mwachindunji popanda kufunikira kutanthauzira, kufotokozera, kapena malongosoledwe. Izo zonse ndi Pakuti Atero Ambuye…MFUNDO!

Ife tonse timavomereza kuti tiyenera kukhala ndi Mawu kuti tikhale Mkwatibwi Wake.

Ine ndikukhulupirira kuti chirichonse chimene ife timachisowa chinalembedwa momwemu Umu, zikungosowa kuti zitanthauziridwe ndi Mzimu Woyera. Ine sindikukhulupirira kuti munthu aliyense pa dziko lapansi ali nawo ufulu woika kutanthauzira kwake kwake ku Mawu. Mulungu samasowa aliyense kuti atanthauzire Mawu Ake. Iye ndi Wodzitanthauzira Iye Mwini. Iye anati Iye akanadzachita izo, ndipo Iye akuzichita izo.

Mwachinvekere, Ambuye walankhula ndi kuulula kwa Mkwatibwi Wake kuti palibe njira ina yokhalira Mkwatibwi Wake wosankhidwa koma kukhala ndi Mawu Ake. Mulungu mwiniwake amatanthauzira Mawu Ake Omwe, ndipo palibe wina amene ali ndi ufulu wowonjezera kutanthauzira kwake pa Iwo.

Mawu amanenanso kuti MNENERI Wake ndiye womasulira Mawu Ake. Iye ndi Liwu la Mulungu kwa anthu. Zimene iye amanena ndi Mawu a tsiku lathu.

Mwa kumvetsera Liwu la Mulungu pa matepi, ife timakhala kuti ulosi ukukwaniritsidwa. Palibe china chilichonse champhamvu kwambiri, chopatulika kwambiri, chokwaniritsidwa kwambiri, palibe changwiro kwambiri kuposa kumvetsera Liwu lotsimikiziridwa la Mulungu likulankhula nanu.

Pamene ena anganene kuti palibe chilichonse ku izo, Mphungu zikusonkhana ndikusangalala ndi chisangalalo chachikulu chopitilira, ndi chitsimikizo kuti zikusunga Mawu a Mulungu. Iye anatiuza ife ngati muli ndi makina a tepi, sonkhanitsani gulu la anthu pamodzi, ndipo sewerani iyo, ndipo mvetserani mwatcheru. Mwa chisomo ndi chifundo Chake, ndicho ndendende chomwe ife tikuchita.

Mulungu watiyitana kutitulutsa ife mu m’badwo woyipa uno chifukwa cha Dzina Lake. Ife tikukumana ndi mayeso ndi mayesero ambiri kuposa kale lonse. Satana ali panjira yomenyera nkhondo monga iye akudziwa kuti nthawi yake ili kumapeto. Inu mungakhoze kumadzifunsa nokha kuti, kodi ine ndingamadutse bwanji mu zinthu zonse izi, ndipo Kodi Ine ndine Mkwatibwi Wake?

Inu muli kupangidwa kuwonetseredwa, kuyesedwa, ndi kutsimikizira kwa Satana, NDIFE MKWATIBWI WAKE. Ndife Mawu mu thupi. Ife tikhoza kulankhula Mawu ndipo izo zidzafika pochitika. Izo Ndi PAKUTI ATERO AMBUYE.

Tili ndi Liwu la Mulungu likulankhula mwachindunji kwa Satana ndi kumuuza iye:

Satana, iwe wagonjetsedwa. Iwe ndi wabodza. Ndipo, monga wantchito wa Mulungu, ndi monga antchito, ife tikulamulira kuti mu Dzina la Yesu Khristu, kuti iwe umvere Mawu a Mulungu, ndipo utuluke mwa anthu, chifukwa izo zinalembedwa, “Mu Dzina Langa iwo adzatulutsa ziwanda.”

Chinalichonse …CHINACHILICHONSE chomwe ife takhala tikuchifuna, ife basi timangofunika kupempha, kukhulupirira ndikukhala pomwepo.Izo Zingawonekere nthawi yomweyo; izo zitha kukhala sabata, mwezi, chaka. Izo zilibe kanthu zomwe ife timawona kapena kumvelera, IZO ZINACHITIKAPO MOTERO KALE.

Utumiki uliwonse womwe ife timasonkhana pamodzi umakula ukukulirakulirabe kwa Mphungu za Mulungu. Ife timasonkhana mu lingaliro Limodzi ndi mgwirizano Umodzi, Ife tikukhala pamodzi m’malo Amwambamwamba, tikumvetsera Liwu likulankhula nafe ndikutipanga ife kukhala angwiro ndi Mawu Ake.

Ife tingakonde kuti inu mudzalumikizane nafe Lamlungu lino pa 12:00 masana, nthawi ya ku Jeffersonville, pamene ife tidzamvaso Liwu la Mulungu likulankhula nafe ndikutibweretsera kutanthauzira kwa Mawu Ake Omwe.

M’bale. Joseph Branham

Uthenga: Mulungu Wa M’badwo Woipa Uno 65-0801M 

Malemba oti muwerenge musanamve Uthenga
Mateyu Woyera mutu wa 24 / 27:15-23
Luka Woyera 17:30
Yohane Woyera 1:1 / 14:12
Machitidwe 10:47-48
1 Akorinto 4:1-5 / mutu wa 14
2 Akorinto 4:1-6
Agalatiya 1:1-4
Aefeso 2:1-2 / 4:30
2 Atesalonika 2:2-4 / 2:11
Ahebri mutu wa 7
1 Yohane mutu wa 1 / 3:10 / 4:4-5
Chivumbulutso 3:14 / 13:4 / mitu 6-8 ndi 11-12 / 18:1-5
Miyambo 3:5
Yesaya 14:12-14

26-0524 Ndi Chiani Chokopa Pa Phiri?

Uthenga: 65-0725E Ndi Chiani Chokopa Pa Phiri?

PDF

BranhamTabernacle.org

Zokondedwa Mphungu Zosonkhana,

Kodi chokopa chachikulu ichi chomwe chikuchitika padziko lonse lapansi ndi chiyani? Anthu ochokera padziko lonse lapansi akusonkhana nthawi ya 12:00 PM nthawi ya ku Jeffersonville, atakhala m’nyumba zawo ndi m’matchalitchi awo ndi chiyembekezo chachikulu, akuyembekezera kumva Liwu la Mulungu likulankhula nawo.

Ndi zachilendo komanso zopanda nzeru kwa dziko lapansi kungomvetsera matepi. Iwo amati ife tikhoza kumva matepi nthawi iliyonse. Palibe chifukwa chomvera nthawi imodzi. Inu Muyenera kumvetsera utumiki wamoyo, mlaliki, osati matepi okha.Iwo akodwa mu miyambo yawo.

Palibe chonga ichi chomwe chinachitikapo mu m’mbiri ya dziko lapansi. Nchiyani chomwe chakopa anthu awa kuti agwirizane onse nthawi imodzi kuti amve Liwu limenelo lakuyitana lomutulutsa kwa Mkwatibwi Wake? Ndi Mulungu akukwaniritsa Luka 17:30. Ndi Mulungu akukwaniritsa Chivumbulutso 10:7. Ndi Mulungu akuwulula Ahebri 13:8, Melkizedeki mu thupi la munthu, monga momwe Iye adachitira kwa Abrahamu.

Iwo akudikira ndi kudabwa, Kodi Iye adzalankhula chiyani? Kodi Chidzachitika nchiyani Iye akadzayamba kulankhula? Iwo amafuna kukhalapo pa kulumikizana Kwa pa telefoni kuti apeze chilichonse chimene Iye akunena. Iwo amafuna icho. Iwo amafuna kuchimva icho chonse nthawi imodzi ndi Mkwatibwi padziko lonse lapansi. Pakuti iwo amakhulupirira kuti iye ndiye liwu limene Mulungu anasankha kukhala Liwu Lke kuti liyitane kumutulutsa ndi kutsogolera Mkwatibwi Wake.

Ngakhale kuti ali kutali kosiyana kwa maola ambiri mu nthawi, koma onse ali pamodzi ngati CHIMODZI, akumvetsera, akumvetsera Liwu limenelo likulankhula nawo kuchokera ku Tchalitchi chawo cha panyumba. Akukhala munkupezekapo kwa Mwana wamamuna, akucha ndikuyembekezera Kubwera kwa Mesiya.

Mitima yawo ikuthamanga. Mzimu Woyera ukuwaulula zomwe zikuchitika. Mulungu wakhala akuyembekezera kufikira mpaka lero kuti awonetse Mawu Ake ndikusonkhanitsa Mkwatibwi Wake. Izo Zikuchitika, ndipo iwo ndi gawo la Izo. Chowonadi cha zomwe zikuchitika chikugwera m’mitima yawo. Iwo awerenga za izo m’Malemba kwa zaka mazana ambiri, koma tsopano ndi zenizeni. Vumbulutso la Mawu likuonekera kudzera mwa iwo. Maulosi a mneneri akukwaniritsidwa.

Pamene iwo akukhala pansi pa kudzoza kwakukulu kwa Liwu Lake lamphamvu, Iye amalengeza kwa iwo kuti akonzekere; pakuti usikuuno Iye apempherera aliyense wa iwo. Iye amatiuza kuti akayamba kupemphera, muyike manja pa odwala, chifukwa Mulungu alipo paliponse, kulikonse komwe ali: ku Texas, ku California, ku Arizona, South America, ngakhale m’nyumba za m’nkhalango mbali ina ya dziko lapansi. Kulikonse kumene iwo akulumikizidwa pa intaneti, ikani manja pa wina ndi mnzake tikayamba kupemphera ndipo Mulungu adzachiritsa aliyense wa iwo, ngati akhulupirira, pakuti Ndi Pakuti Atero Ambuye.

Iwo akumvetsa tsopano kuti m’mibadwo yonse ndi mneneri aliyense amene anakhalapo kapena amene adzakhalapo, padzakhala anthu enaake omwe adakonzedweratu kuti amve Uthenga umenewo, ndipo amenewo adzautsatira iwo. Iwo Sadzavomera gulu. Iwo Sadzavomera ndi kutsutsidwa kwa wosakhulupirira amene amati ndi njira yolakwika kapena si njira yoperekedwa ndi Mulungu. Iwo alibe mkangano ndi iwo.Iwo ali ndi chinthu chimodzi chomwe AYENERA KUCHITA, ndicho kukhulupirira ndipo kuti apeze gawo lililonse la Iwo momwe iwo angathere, kuulowetsamo monga Mariya amene anakhala pa Mapazi a Yesu. Iwo Sachita manyazi, iwo amanyadira kwambiri kunena kuti iwo ndi mnyamata wa tepi kapena kuti mtsikana wa tepi amene amakanikiza kusewera.

Liwu limenelo lawachenjeza kale kuti padzakhala odzozedwa pa nthawi yotsiriza omwe adzakhala ndi kudzoza kwakukulu, Mzimu Woyera. Adzatchula mobwereza mneneri ndi Uthenga wa nthawiyo; akunena kuti ndi okhulupirira, koma ali odzozedwa abodza.

Iwo adzakhala pafupi kwambiri ndi kudzoza kwenikweni komwe kukadati kunyenge osankhidwa omwe ngati n’kotheka, koma Iwo akudziwa kuti iwo sanganyengedwe, chifukwa iwo NDI MAWU. Iwo ndi Mkwatibwi weniweni amene anakhala ndi Mawu a Mulungu.

Liwu limenelo likulengeza kwa iwo kuti mu tsiku lino ilo Silidzakhala ndimu, kapena mphesa. Zimenezo zingakhale zosavuta kuzindikira kusiyana. Koma lidzakhala tangelo, theka la ndimu, theka la lalanje, mtundu wosakanikirana. Lidzawoneka ngati lalanje, koma silidzakhala lili ilo, chifukwa nthambi yatsopanoyo idzakhala handiredi peresenti ngati yapachiyambi. Iwo ADZAKHALA ndi Liwu Mawu apachiyambi. Iwo sadzatenga mlowammalo. Iwo Adzakhala ndi iye amene, Mulungu mwini wake adalengeza kuti ndi LIWU LAKE, MAWU AKE, otsimikiziridwa ndi Lawi la Moto.

Kodi chikuchitika nchiyani?

Mbewu ya Mulungu yokonzedweratu singachite china chilichonse koma kutsatira ndi kumvetsera Liwu limenelo, chifukwa limatanthauza zambiri kuposa moyo kwa iwo. Inu mukhoza kutenga miyoyo yawo, koma inu simungathe kutenga Liwu limenelo.

Kodi chokopa ndi chiyani?

Mulungu, monga mwanthawi zonse, akukwaniritsa Mawu Ake.

Bwerani mudzalumikizane nafe ndikukhala gawo la ulosi wa mneneri womwe ukukwaniritsidwa Lamlungu lino pa 12:00 PM, nthawi ya ku Jeffersonville, pamene tikumva Malemba akuwonetseredwa.

M’bale Joseph Branham

Uthenga: 65-0725E “Kodi Ndi Chiyani Chokopa Pa Phiri?”

Malemba:
Mateyu Woyera 21:1-4
Zekariya 9:9 / 14:4-9
Yesaya 29:6
Chivumbulutso 16:9
Malaki 3:1 / Mutu wa 4
Yohane Woyera 14:12 / 15:1-8
Luka Woyera 17:22-30

26-0517 Iwo Odzozedwawo Pa Nthawi Yotsiriza

Uthenga: 65-0725M Iwo Odzozedwawo Pa Nthawi Yotsiriza

PDF

BranhamTabernacle.org

Zokondedwa Mphungu Zosonkhana,

Mutu wokha wa Uthenga wa sabata ino ukuwulula kuzindikira Mzimu Woyera kwa Mkwatibwi. Kuganiza kuti padzakhala amuna odzozedwa enieni omwe adzauka m’masiku ano, ndi kudzoza kwenikweni kwa Mzimu Woyera womwewo womwe unali pa mneneri wathu, koma kukhala abodza.

Mawu amatiuza kuti adzachita zizindikiro ndi zodabwitsa, kulandira mvula yomweyo, madalitso omwewo monga mneneri weniweni. Anthu adzasiya Mawu enieni otsimikiziridwa a tsikulo kupita ku zilakolako zawo, kudziunjikira aphunzitsi, okhala ndi zoyabwa mmakutu. Zidzakhala pafupi kwambiri ndi Mawu enieni mpaka zidzangokhala pafupifupi kunyenga Osankhidwa.

Kodi kudzoza kumeneko kudzakhala pafupi bwanji? Kodi zidzakhala zosavuta kuzindikira chomwe chili chowonadi ndi chomwe chili chabodza? Mneneri anatiuza kuti Mfumu Davide, munthu wotsatira mtima womwe wa Mulungu, wokhala ndi kudzoza pa iye, adapeza vumbulutso loona; koma ilo linali lolakwika.

CHIYANI!! Lolani chimenecho chilowe mkati mwakanthawi. Mfumu yosankhidwa ndi Mulungu inali ndi kudzoza kwenikweni ndi vumbulutso loona, koma linali lolakwika! Ana a nkhosa a Mulungu ayenera kukhala maso kwambiri kuti adziwe kuti zomwe akumva ndi kudzoza koona kapena kwabodza; pakuti malo awo amuyaya akupumulira pa zigamulo izi.

Ife tikudziwa kuti Mulungu waika atumiki ambiri odzozedwa kuti athandize kutsogolera ndi kusunga Mkwatibwi Wake m’Mawu. Mawu Ake amanena choncho, ndipo ife tili oyamikira kwambiri Ambuye chifukwa cha aliyense wa iwo. Iwo ayitanidwa kukhala abusa pa nkhosa zawo.Iwo ayenera kuwasunga iwo m’Mawu. Pochita izi, iwo sayenera kulephera kusewera Liwu Lokhalo lotsimikiziridwa la Mulungu kwa nkhosa zawo.

Monga momwe ife tangomvera kumene momwe munthu aliyense angalakwire, ngakhale ali ndi kudzoza koona ndi vumbulutso loona. Koma Mkwatibwi akhoza kukhala otsimikiza konse, chifukwa Mulungu wapereka njira yangwiro yomwe iwo nthawi zonse angakhoze kuti amve KUDZOZA KOWONA, VUMBULUTSO LOWONA, PAKUTI ATERO AMBUYE WOWONA; KOKHA KANIKIZANI KUSEWERA.

“Kumene kuli Nyama,” Manna ali, Mawu ali, “kumeneko mphungu zikakhala zitasonkhana.

Kumene kuli Nyama, kumeneko ndi komwe ife Mphungu tidzasonkhanako. Kumene kuli Nyama yatsopano, Mawu amu nyengo, Uthenga wa ola. Ndipo palibe malo atsopano odyera Manna amenewo kuposa kumva Liwu la Mulungu akulankhula Iyemwini.

Awo ndi Mawu Ake. “Munthu sadzakhala moyo ndi mkate wokha, koma ndi Mawu onse.” Mwaona? Okonzedweratu amadziwa izi. “Mawu achirendo, kapena liwu lachirendo, iwo sadzalitsatira.”

Chifukwa chomwe ife sitidzanyengedwa, ndipo sitinganyengedwe, ndi ndichifukwa chakuti ife ndife Mawu omwe ali ndi vumbulutso ili. Ife sitingakhale china chilichonse. Ife sitingamve china chilichonse. Ife Sitikudziwa china chilichonse.

“INE NDINE!” Osati “Ine ndinali, kapena ndidzakhala ndiri.” INE NDINE,” tensi yapakalipano, Mawu tsopano. Osati Mawu amene analipo, kapena Mawu amene ati adzabwere; Mawu amene alipo tsopano. Mwaona? Inu mwamvetsa zimenezo? “INE NDINE!” “INE NDINE” ali Mawu. “Pachiyambi panali Mawu, ndipo Mawu anali ndi Mulungu.” Ndi kulondola uko? “INE NDINE.” “Mulungu anandituma ine monga mneneri Wake, kuti ndidzatsimikizire izi kuti ziri zoona. Ine ndine yankho kwa Mawu awa, chotero, pamene Iye anabwera pansi pano ndi kuchita izi.”

Ndipo pamene iye anachita izo, Farao anati, “Chabwino, ife tiri nawo anyamata ochuluka mu gulu lathu amene akhoza kuchita zimenezo, nawonso,” osanzira.

Yesu anati, “Tsopano, izo zidzabwereza kachiwiri mu masiku otsiriza,” onani, kumadzitcha chinthu chomwecho.

Ambuye alemekezeke. Kakamba za chitsimikizo cha Mkwatibwi. Pomwe inu mukhala ndi Vumbulutso ili, ndiyeno inu mudzadziwa kuti inu muli wosankhidwa Wake, Okonzedweratu , Mkwatibwi wake wokomamtima.

Mwa kumvetsera Liwu la Mulungu pa matepi, ife tikumvetsera Mwana wa Munthu, amene ndi Khristu. Iye ndiye amene ife tikumudya. Ife sitikudya munthu; munthu, mawu ake adzalephera. Koma ife tikudya Thupi la Mawu a Mwana wa Munthu losalephera.

Ngati inu mukufuna kukhala otsimikiza Wani Handiredi peresenti kuti inu mukumvetsera ku Pakuti Atero Ambuye, bwerani mudzakhale nawo gawo la Mkwatibwi Lamlungu lino pa 12:00 PM, nthawi ya ku Jeffersonville, pamene ife tikumva Liwu la Mulungu likutiululira zonse zokhudza iwo odzozedwa ps nthawi yotsiriza.

M’bale. Joseph Branham

Uthenga: Iwo  Odzozedwawo Pa Nthawi Yotsiriza 65-0725M  

Malemba Opatulika:
Mateyu Woyera 5:44-45 / 7:21 / 24:15-28
Luka Woyera 17:30 / 18:1-8
Yohane Woyera 14:12
Aefeso 1:5
2 Timoteo 3:1-8
Ahebri 6:1-8 / 11:4
Chivumbulutso 10:1-7 / 16:13-14
Malaki 4:5
1 Mafumu 22:1-28
Yeremiya: Machaputala 27 ndi 28

26-0510 Tsiku La Anakubala

Uthenga: 59-0510M Tsiku La Anakubala

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mkwatibwi,

Tsopano, ine ndikuganiza kuti palibe kulemekeza kokwanira kumene tikanakhoza kupereka kwa mayi.

Mayi athu ndiye oyamba nafe, ndipo anapatsidwa udindo waukulu wa zomwe ife tidzakhale komanso njira yomwe ife tiyenera kuyendamo. Iye anapatsidwa udindo kuchokera Kwa Mulungu woti atiyike ife panjira yoyenera. Ndicho chifukwa chake mayi ali nako mwapadela , kukhudza kochepa komwe kwapatsidwa kwa iye kuchokera kwa Mulungu.

Ndi dalitso lapadera bwanji lomwe lili mu nkhokwe la ife la Lamlungu lino, pamene ife tikupereka ulemu kwa Amayi onse, pamene ife tidzamva mngelo wachisanu ndi chiwiri wa Mulungu akufotokoza chikondi ndi ulemu womwe amayi athu ali nawo m’mitima mwathu.

Ife tikudziwa kuti tsiku lililonse ndi Tsiku la Anakubala, koma Lamlungu lino tidzapereka ulemu wapadera kwa Amayi onse pamene ife tidzamva mneneri wathu akupereka ulemu kwa iwo monga momwe iye adayankhula zaka 67 zapitazo pa tsiku lomwelo lofanana , pa 10 Meyi , 1959.

M’bale Joseph Branham

Uthenga: Tsiku la Anakubala 59-0510M

Nthawi: 12:00 P.M. Nthawi ya ku Jeffersonville

Malemba Opatulika: 1 Akorinto 15:1-4

26-0503 Chakudya Chauzimu Mu Nyengo Yake

Uthenga: 65-0718E Chakudya Chauzimu Mu Nyengo Yake

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mkwatibwi,

Liwu lomwe ife tonse timakonda kumva lidzalankhula Lamlungu lino, ndipo lidzatibweretsera ife Uthenga Wapadera wa Kalata Yachikondi, wa Mkwatibwi wa Yesu Khristu yekha.

Liwu limenelo linangolankhula ku dziko lapansi ndikuwachenjeza iwo kuti, “Musayese kundichitira Ine ntchito mopanda kukhala chifuniro Changa. Ndili ndi njira yangwiro yoperekedwa imene ine ndakupangirani inu, Mkwatibwi Wanga. Kumbukirani Mawu Anga, inu muzingonena zimene Ine ndalankhula pa matepi Anga, chifukwa inu mukulowa mu chiweruzo. Chifundo chakanidwa. Koma kondwerani, ndipo khalani oyamikira, chifukwa ine ndapereka ndi kukupatsani inu Chakudya Chobisika, Chakudya Chauzimu, kuti inu mukhale ndi moyo pa ubwino ndi chifundo cha Vumbulutso la Yesu Khristu.

Tsopano muli chilala m’dzikololi lomvera Liwu Langa . Iwo samakumvetsani inu chifukwa inu mumati ndinu anthu a Tepi, ndipo mukufuna kungomva Liwu Langa pa Matepi; koma ndakuitanani kukutulutsani inu ndipo ndakuwululirani inu njira Yanga yangwiro yoperekedwa ya lero.

Inu simunadziphatikize ndi osakhulupirira panthawi ya chilala. Ine ndakupatsani Liwu Langa kuti likuthandizeni. Mwa kusewera Liwu Langa, mgolo wanu siwudzapita wopanda kanthu, ngakhale mtsuko wanu siwudzauma, mpaka tsiku limene ine ndidzabwera ndikukutengani ngati Mkwatibwi wanga.

Ndicho chifukwa chake Ine ndinali ndi Liwu Langa likujambulidwa, kotero kuti inu muKhale ndi malo angwiro operekedwa oti mupiteko, komwe kulibe cholakwika, palibe chifukwa chofuna kutanthauzira, basi Liwu Loyera la Mulungu. Malo omwe mungapiteko kuti mumve ndendende zomwe Ine ndanena: Pakuti Atero Ambuye.

Ine ndidzalankhula nanu momveka bwino Lamlungu.Ine Ndikufuna kuti inu musadzaiwale zomwe ndidzalankhule nanu. Matepi awa ndicho Chakudya Chanu Chauzimu mu Nyengo Ino. Ndi cholemera kwambiri kwa ena a iwo; sangathe kuchidya icho. Icho sichinawululidwe kwa iwo, koma Ine ndakusankhani INU, ndipo ndakupatsani inu Vumbulutso la njira Yanga Yangwiro yoperekedwa.

Kwa inu, Ndi Chakudya Chobisika, komwe mukukhala ndi ubwino ndi chifundo cha Mawu Amoyo.

Pamene Ine ndinali kukhala m’thupi mwa Mwana wanga wa mamuna, iwo mophweka sanathe kuvomereza yemwe ine ndinali: Mulungu ndi munthu. Kenako ine ndinalonjeza kuti ndidzabweranso m’masiku otsiriza ndikukhalanso m’thupi la munthu monga momwe ndinachitira Abrahamu asanakhalepo, ndipo ine ndidzatsika pansi ndikudziveka ndekha m’thupi la munthu monga momwe ine ndinachitira nthawi imeneyo.

Izi ndi zomwe iwo adaphonya, nthawi imeneyo ndi tsopano, koma ine sindikufuna kuti inu muiwale. Chakudya chosungidwa chimene ine ndikukudyetsani inu, ndi mthenga wanga, ndi ofanana. Inu Simungathe kuwalekanitsa iwo. Uthenga ndi mthenga ndi ofanana.Ine ndinakuuzani inu m’Mawu Anga zomwe ndikanachita mu tsiku ili. Ndicho chifukwa chake ndi chifuniro changa kuyika Liwu Langa m’matchalitchi anu, m’nyumba zanu, kulikonse komwe inu mupita; chifukwa ndilo Liwu lofunikira kwambiri lomwe inu muyenera kumva. Ndi Liwu LOKHALO lotsimikiziridwa lomwe limalankhula Pakuti Atero Ambuye.

Chifundo chakhala chikukanidwa. Tsopano inu mukukhala pa Mawu Anga.Ine ndakupatsani inu Vumbulutso la yemwe Ine Ndili ndi yemwe INU muli. Sipayenera kukhala mthunzi umodzi wa kukayika m’mitima ndi m’maganizo mwanu. Inu ndinu Mkwatibwi Wanga Wosankhidwa, Wosankhidwiratu, Wokonzedweratu. Ndinu Mawu Anga Olankhulidwa omwe anali mwa Ine pachiyambi.

Inu muli ndi mwayi wopeza Chakudya, Chakudya Chauzimu, chomwe dziko lapansi silikudziwa kalikonse.

Inu muli ndi mwayi wopeza machiritso a matupi athu pamene madokotala alephera; Ndi chimodzi mwa Zakudya zomwe ine ndinalonjeza ndi kukupatsani inu m’masiku otsiriza.

Ine ndinalonjeza kuulula zinsinsi za mitima yanu ndikuchita izi. Ine ndiri mwa inu. Inu ndinu gawo la Ine, ndipo Ine ndine gawo la inu. Zizindikiro izi zidzawatsata iwo amene akhulupirira.

Lamlungu lino Ine ndidzakhala ndikugwirizanitsa Mkwatibwi Wanga kuchokera kuzungulira pa dziko lonse lapansi ndi Liwu Langa. Ine ndidzakuwuzani inu kuti muyike manja anu pa wina ndi mnzake. Musadzadzipempherere nokha, mudzapempherere amene mwamusanjika manja anu pa iye, chifukwa iwo akukupemphererani inu. Ife tidzapemphera limodzi, ndipo sipadzakhala munthu wofooka kulikonse padziko lonse lapansi ngati inu mudzakhulupirira.

Ngati inu mukhulupirira, ndipo mulibe kukayika mumtima mwanu,Ine ndidzalengeza:

Satana, iwe wagonjetsedwa! Yesu Khristu anakugonjetsa iwe! Iye anawuka kwa akufa ndipo akuyima pakati pa ife usikuuno, kutsimikizira Uthenga uwu wa masiku otsiriza. Tuluka mwa anthu awa! Asiye iwo, mu Dzina la Yesu Khristu! “Mu Dzina Langa iwo adzaturutsa adierekezi,” ndipo iwe watulutsidwa. Mu Dzina la Yesu Khristu asiye osonkhana awa!

Padzakhala machiritso akuchitika kuzungulira pa dziko lonse lapansi kuposa kale lonse.

Ife tikanamayembekezera chifukwa chiyani mwa kutalika kwinanso, m’bale wanga wokondedwa, mlongo, pano Iwo uli, Mzimu Woyera, Mulungu, pano pomwe, chinthu chomwecho ife timachikamba.

Ine ndikuyitana dziko lonse lapansi kuti lidzabwere kudzalumikizana nafe Lamlungu lino pa 12:00 PM, nthawi ya ku Jeffersonville, ndikudzamva Uthenga ndi mthenga Wake akutibweretsera ife Chakudya Chauzimu Mu Nyengo Yake, Chakudya Chobisika cha Mkwatibwi.

M’bale Joseph Branham

Uthenga:  Chakudya Chauzimu Mu Nyengo Yake 65-0718E 

Mthenga: M’busa . William Marrion Branham

Malemba Opatulika: 1 Mafumu 17:1-7 / Amosi 3:7 / Yoweli 2:28 / Malaki 4:4 / Luka 17:30 / Yohane Woyera 14:12