Category Archives: Uncategorized

23-0402 Mkwatulo23-0402

Uthenga: 65-1204 Mkwatulo

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mawu Pamwamba pa Mawu,

Mipingo yambiri ikudabwa, kusokonezeka, kusokonezeka, kukhumudwa, kusokonezeka, kusokoneza komanso ngakhale kudodometsa zomwe zikuchitika ndi “Anthu a Matepi” awa ochokera padziko lonse Lamlungu lililonse.

Ndiwo Mgwirizano Wosaoneka Wa Mkwati Wa Khristu, atakhala mu Kukhalapo kwa Mwana, akucha, kudzikonzekeretsa tokha. Mkwati Wathu Wakumwamba wakhala akutiuza zonse za Kwathu Kwamtsogolo ndi Iye.

Masabata angapo apitawo anatiuza kuti: “Dziko lino si Kwanu, ndi Edeni wa Satana, ndipo ndidzaliwononga ndi moto. Ndiwe wokondedwa Wanga, amene Ine ndakusankha asanaikidwe maziko a dziko kuti akhale Mkwatibwi wanga. Tsopano, Lamlungu lino Ine ndikuwuzani inu nonse za Mkwatulo Wanga umene ukubwera posachedwa.”

Tili pansi pa chiyembekezo chachikulu chotere. Tikhoza kumva mumlengalenga. Zinthu zikuchitika mofulumira kwambiri.

Basi zomwe Baibulo linanena kuti zikanadzachitika mu tsiku lino, zikuchitika, tsiku ndi tsiku. Bwanji, zikuchulukana mofulumira kwambiri kunja uko, mu zipululu izo, ndi zinthu zikuchitika, mwakuti ine sindimakhoza nkomwe kupitiriza nazo izo. Ife tiri pafupi ndi Kudza kwa Yesu, kuti tidzalumikizana ndi Mpingo Wake, kumene Mawu amakhala Mawu.

Izi zonse zikuchitika kwa ife, Dona Wake Wosankhidwa, Mkwatibwi wa tsiku lino. Ndife tokha amene timawona zinthu izi zikuchitika.

Iye watikonzeratu ife ku m’badwo uno ndipo palibe wina aliyense amene angatenge malo athu. Ife tsopano ndife ana aamuna ndi aakazi owonetseredwa kotero kuti ife tikhoza kuyanjana ndi Iye; ndicho chimene Iye akufuna.

IFE NDIFE Mawu pamwamba pa Mawu, nyongolosi pamwamba pa nyongolosi, Moyo pamwamba pa Moyo, ndi thunthu lathunthu la Mkwati wa Ambuye Yesu Khristu.

Ngati inu muli nacho chomufuna, yankhulani Icho. Inu ndinu Mawu pamwamba pa Mawu. Musayang’ane mdima wa dziko lotizinga; matenda, matenda, kupha, kuthedwa nzeru, misala ya anthu amene sadziwa ngati ali mwamuna kapena mkazi. IFE NDIFE MKWATII, wokonzedweratu, wolungamitsidwa, Mkwatibwi wowonetseredwa wa Ambuye Yesu Khristu.

Osawopa kalikonse. Khalani okondwa ndi kusangalala. Nthawi yayandikira. Tikukonzekera kuchoka mnyumba yazirombo iyi, ULEMERERO!!!

Bwerani mudzakonzekere nafe ku Mkwatulo, Lamlungu pa 12:00 p.m., nthawi ya Jeffersonville. Simudzakhalanso chimodzimodzi.

M’Bale . Joseph Branham.

23-0326 Chilumikizo Chosawoneka Cha Mkwatibwi Wa Khristu

Uthenga: 65-1125 Chilumikizo Chosawoneka Cha Mkwatibwi Wa Khristu

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Dona Wosankhidwa,

Kodi mungapatse chiyani kuti Ambuye Yesu abwere kunyumba kwanu Lamlungu lino, kukhala pansi pa kama panu, kuyang’ana inu m’maso mwanu ndikulankhula ndi inu mwachindunji?

Simunathe kulankhula. Simukufuna kulankhula. Chomwe mungafune kuchita ndikungoyang’ana pa Iye ndi kulira. Mumaopa ngakhale kutsegula pakamwa panu. Kodi munganene chiyani? M’maganiso anu inu munkhala mukuganiza, Ambuye, ine sindine woyenera kuti Inu mukhale muno mu nyumba yanga. Ndine wotsikitsitsa mwa otsika. Ndakulepherani nthawi zambiri, Ambuye, koma Ambuye, ndimakukondani kwambiri.

Mukadzazindikira mu mtima mwanu, Iye akudziwa ndendende zomwe ndikuganiza, palibe chobisika kwa Iye. Iye amadziwa zinsinsi zomwe za mtima wanga.

Pamene muyang’ana m’Maso Ake amtengo wapatali, mumawona chikondi choterocho ndi chifundo. Angakhale akulankhula kwa inu osatsegula nkomwe pakamwa pake. Mungakhale mukuganiza, Iye ali pano, m’nyumba mwanga, ndi ine.

Mtima wanu ungayambe kuthamanga kwambiri, pamene munawona kuti Iye ali pafupi kunena chinachake kwa inu. Zonse mwakamodzi, Liwu lokoma kwambiri lomwe inu mukalibe mwalimvapo likanati, “Wokondedwa wanga wapamtima, usadandaule, dzina lako liri pa Bukhu la Moyo wa Mwanawankhosa Wanga. Osati bukhu lakale la chilumikizano chanu chachirengedwe, koma Bukhu Langa la Mkwati latsopano. Ndi satifiketi yaukwati wanu ndi Ine.

Wokondedwa wanga, simunakhululukidwe machimo anu onse ndi zolephera zanu zokha, koma kwa Ine, ndinu WOLUNGAMA. M’maso Anga, simunachitepo cholakwika chilichonse.

Ndiwe mwana Wanga wamtengo wapatali, wabwino, wopanda uchimo. Inu mwaima woyera; Mkwati Wanga wosaipitsidwa yemwe watsukidwa ndi Madzi a Magazi Anga Omwe.

Pasanakhale ngakhale mwezi, nyenyezi, kapena molekyu, munali Mwana Wanga ndi mwana wamkazi. Inu ndinu mawonetseredwe a thupi la zikhumbo zomwe zinali mwa Ine pachiyambi.

Jini lanu lauzimu linali mwa Ine chifukwa ndinu chionetsero cha makhalidwe Anga, maganizo Anga. Inu munali ngakhale mwa Ine asanaikidwe maziko a dziko.

Inu ndinu Mkwati Wanga wauzimu yemwe wakhala ali mu Kukhalapo kwa Mwana, akucha, pakumvetsera ku Mawu Anga. Tsopano mwayamba kukhala ndi chitsitsimutso, kubwereranso ndi kudzifoletsa nokha ndi Mawu Anga. Ndinu Mkwati Wanga Wosankhidwa.

Tsopano muli ndi mgwirizano wauzimu ndi ine. Thupi lanu likukhala Mawu, ndipo Mawu akukhala thupi; kuwonetseredwa ndi kutsimikiziridwa. Zomwe ndidakuuzani kuti zichitike mu tsiku lino, zikuchitika, tsiku ndi tsiku. Mawu kukhala Mawu.

Inu muli nalo Vumbulutso loona la tsiku lotsiriza lino: kusonkhanitsa kwa Mkwati Wanga pamodzi mwa Uthenga uwu. Palibe m’badwo wina umene ine ndinaulonjeza Iwo. Ine ndinalonjeza Izo kwa inu, mu m’badwo uno: Malaki 4, Luka 17:30, Yohane Woyera 14:12, Yoweli 2:38.

Tidzakhala ndi Phwando lachiyamiko Lamlungu lino pamene ndidzakuuzani zambiri. Ndikhala ndi inu maola ambiri, ndikuyanjana ndi kudya pa Mawu Anga. Ndikutsimikizirani kuti pakukhala ndi Mawu Anga, mneneri Wanga, Mawu Anga, kutyanka kuliza, muli mu Chifuniro Changa chabwino.

Ine ndinawauza iwo mu Mawu Anga, Ine ndaima pakhomo, ndipo ndikugogoda. Ngati wina amva MAU anga, nakatsegula chitseko, ndidzalowa kwa iye, ndipo ndidzadya naye, ndi iye ndi Ine. Ambiri sangamve ndikutsegula chitseko chawo, koma mwa Chivumbulutso, mwatsegula chitseko chanu ndikundilandira Ine mkati.

Sagwirizana ndi kuliza Mawu Anga m’mipingo yawo. Ngati iwo analeka Mzimu Woyera ufufuze mumaganozo awo ndi Mawu, iwo agati anavomereza. Kumuleka Khristu, Mawu odzozedwa, afufuze chikumumtima chanu chomwe. Mulekeni Iye alowe mwa inu, muwone ngati Izo ziri zolondola kapena ayi.

Ine ndinakuuzani inu kuti sichizankhala chipembedzo kumibweretseni inu pamodzi, iwo sangakhoze nkomwe kugwirizana pa Mawu amodzi kapena awiri mu Baibulo. Kodi ine ndinayamba ndakuuzanipo inu kuti lidzakhala gulu la amuna? Ayi! Ine ndinakuuzani inu kuti Iwo unali Uthenga wa Munthu MMODZI; ndipo mudamvera ndi kumvera.

Popeza sanamvere ndi kuvomereza pulogalamu yanga yoyambirira kuyambira pachiyambi, ndinawatumizira alaliki, aphunzitsi, atumwi, abusa ndi aneneri. Koma iwo anatumizidwa kuti akaloze anthu KUBWERA ku pulogalamu yanga yoyamba ndi yabwino, Mngelo Wanga wamphamvu. Pakuti Ilo ndi Liwu la Mulungu kwa inu.

Iwo ndi odzozedwa, koma ine ndiri ndi MNENERI MMODZI MTUMIKI OTI AKUTSOGOLERI INU. MZIMU WOYERA NDI MNENERI. Kodi Ine sindinakuuzeni inu nthawi zambiri, MAWU ANGA OLANKHULA KUPYOLERA MWA IYE SAFUNA KUTANTHAUZIRA, OSAWONJEZERA KAPENA KUCHOTSA CHONCHO CHILICHONSE CHONENA, AKUNGONENA ZIMENE IYE ANANENA PA MATEPI AWO? Ameneyo ndi mneneri, Mzimu Woyera akukutsogolerani inu.

Iye ndi amene Ine ndinamutuma kuti adzakuitane iwe kuti ukhale Mkwati Wanga. Iye ndi amene adzakuonetseni kwa Ine. Iye ndi yemwe ine ndinayima naye pamene ine ndinamuwonetsa iye chithunzithunzi cha inu, Mkwati Wanga. Ine ndinakuuzani inu zonse za iye mu Chivumbulutso pamene ine ndinati, INE Yesu ndatumiza NGELO WANGA kuti adzachitire umboni kwa inu zinthu izi MU MIPINGO. Ndi INE, ndikungogwiritsa ntchito thupi lake ndi mawu ake kulankhula nanu. ”

Ndi tsiku lodabwitsa bwanji lomwe ife tikukhala limodzi ndi Iye. Sitinakhalepo osangalala kapena okhutira kwambiri m’mimweo yathu. Ichi ndi Ichi. Izi ndi zomwe takhala tikuyembekezera kwa moyo wathu wonse.

Mulibe mthunzi wa chikaiko m’mitima mwathu kapena m’maganizo mwathu. Pakuti ndi Uthenga uliwonse umene timamva, Iye amatiuza ife tiri mu chifuniro Chake chabwino. Pali Liwu limodzi lokha limene lidzakuyanjanitseni inu, kukupangitsani inu kukhala angwiro, ndi kukubweretsani inu pamodzi…Ine, INE NDIKULANKHULA KUPITILA MNENERI WANGA. OSATI MAWU AKE, MAWU ANGA. NDI NJIRA ANGA WOPEZEKA.

Gome yafalikira. Ilo ladzaza ndi kabichi, ndi mpiru, ndi radishes…MAWU PAMWAMBA PA MAWU, PAMWAMBA PA MAWU. Tidzakhala ndi Phwando lakuthokoza kuchila kale lonse. Padzakhala chisangalalo padziko lonse lapansi pamene Mkwati adzasonkhana mozungulira pamagome awo kuti amvetsere ku Liwu la Mulungu likulankhula kwa iwo. Nyumba zathu ndi mipingo idzadzazidwa ndi kupezeka kwake. Tidzakhala osalankhula kupatula Ulemerero wathu, Aleluya, lilemekezeke dzina la Yehova.

Bwerani mukhale gawo la Msonkhano wa Chiyamiko cha Banja la Mkwati, pamene Iye atidyetsa. Musachedwe, pamene tidzayamba kuchita phwando Lamlungu, ndendende 12:00 P.M., nthawi ya Jeffersonville. Iye adzakhala ali kumeneko, pakuti Iye anandiuza ine kuti Iye azankala pamene.

NDIZABWELA ndipo ndikhala ndikukuuzani zonse za Mgwirizano Wanu Wosaoneka Wa Mkwati Wa Khristu 65-1125.

Ndidzakuwonani pa gome.

M’Bale . Joseph Branham

AKA: Mkazi Wake Wosankhidwa.

23-0319 Kusankha Kwa Mkwatibwi

Uthenga: 65-0429E Kusankha Kwa Mkwatibwi

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa umozi mu Miliyoni,

Ndakhala ndikulidirirani nthawi yayitali. Ndinu wokondedwa Wanga wokondedwa, ndipo ndimakukondani kwambiri. Monga ndinakulonjezani, ndakhala ndikukupangilani Nyumba yatsopano kumene Tidzakhala pamodzi Muyaya. Ndapanga chilichonse chimodzimodzi monga inu mumakonda iwo.

Ine ndikhoza tsopano kuyang’ana pa inu ndi kuwona, inu ndinu chinyezimiro cha Ine. Inu muli ndi khalidwe Langa lomwe, mnofu Wanga, Mafupa Anga, Mzimu Wanga womwewo, Chirichonse Changa chomwecho, chimodzimodzi basi. mwakhala amodzi ndi Ine.

Ndinatumiza mngelo Wanga wamphamvu padziko lapansi kuti adzakuitaneni kuti utuluke mu Edeni wa Satana. Ine ndinamutuma iye kotero kuti akakhoze kufotokoza maganizo anga, makhalidwe Anga, ndi kukuuzani inu za zinthu zimene ziri kubwela. Ndinasebenzesa kamwa kake ndi mawu ake pofotokoza. Pabuyo ponena izo, Ine ndinazifikitsa izo, chifukwa Miyamba ndi dziko lapansi zidzapita, koma Mawu Anga kwa inu sadzalephera konse.

Ndinadziwa kuti pamene munandimva Ine ndikulankhula, kusebenzesa mawu a mngelo Wanga, mudzadziwa mkati mwa mtima wanu, amene sanali iyeyo, amene anali kulankhula ndi inu. Ndinali Ine ndikukutumizirani kalata yachikondi, ndikukuuzani inu, Ine ndakusankhani inu kuti mukhale Mkwati wapamtima Wanga wokondedwa.

Pamaso panga palibe wina monga imwe. Palibe amene angatenge malo anu. Wakhala woona ndi wokhulupirika kwa Ine. Ndikayang’ana pa inu, Mtima wanga ukusefukira ndi chisangalalo.

Ndikakuuzani, samalani kwambiri wokondedwa, zomwe mukumvera, padzakhala odzozedwa ambiri omwe amagwiritsa ntchito Mawu Anga, koma ndi abodza. Munamvetsetsa chenjezo Langa la Chibvumbulutso ndipo munakhala boona ndi wokhulupirika ku Mawu Anga.

Ndinanyadira kwambiri pamene munapemphera mowona mtima za mpingo umene mumasonkhana nawo. Ndinakuuzani kuti mupange chisankho choyenera, ndikukupatsani zitsanzo za zomwe mpingo wanbwino uli. Munakumbukira pamene ndinanena kuti onse amanyamula mizimu, ndikusankha mpingo wanbwino.

Ndinakuuzani kuti samalani kwambiri ndi m’busa wanu. Kotero inu mungolingalira mmene mtima Wanga unalumpha ndi chisangalalo pamene ndinakuona mukukhala ndi abusa amene ndinatuma kuti akubweretseni inu kwa Ine. Inu mumadziwa kuti unali Mzimu Wanga Woyera ukukhala mwa mneneri Wanga kuti akutsogolereni inu kwa Ine.

Ndikukumbukira tsiku limene munali okondwa kwambiri, ndi kukondwa kwambiri, pamene ndinaitana mngelo Wanga pamalo okwezeka kuti ndimusonyeze chithunzithunzi cha inu. Tinayima pamenepo ndikukuwonani mukamaguba nyimbo ya
Patsogolo asilikari Achikhristu pamaso pathu.

Iye anakonda momwe inu nonse munabvala mu zobvala za mtundu wanu kuchokera kumene inu munachokera; monga Switzerland, Germany, ndi padziko lonse lapansi. Lililonse mu tsitsi lanu lalitali lomwe linali lokonzedwa bwino kwambiri. Masiketi anu anali pansi bwino. Ndinali wonyada ndi wokondwa kukuwonetsani inu nonse kwa iye, kotero kuti abwerere ndikukulimbikitsani ndikukuuzani kuti adakuwonani Kumeneko.

Liso lirilonse linali pa Ife. Pamene atsikana ochepa, kumbuyo kwa mzerewo, anayamba kuyang’ana malo ena, anakuwa kuti, “Usachite zimenezo! Osachoka pa sitepe!

Pamene ndinakuuzani kuti ndikusungirani chakudya kuti mudye, munadziwa bwino zomwe ndikunena. Inu mumafuna kukhala Mkwati Wanga wa Namwali wa Mawu Anga. Sindinagwirepo ukucheza ndi wina aliyense. Nthawi zonse ndinali Ine, Mawu Anga. Zimenezo zinandisangalatsa Ine kwambiri.

Ndakusankhani, IWE, kuti ukhale Mkwati Wanga. Inenso ndimakukondani kwambiri, monga mmene mumandikondera Ine. Musataye mtima, khalani olimbikitsidwa, sangalalani, sangalalani, tsiku likuyandikira lomwe ndidzabwera kudzabwera kwa inu. Ndi nthawi yodabwitsa bwanji yomwe Tidzakhala nayo.

Kwa nonse a inu, LAPANI, dziko lapansi likuomba. Tsiku lina Los Angeles adzakhala ali pansi pa nyanja, monga ine ndinakuuzani inu kuti izo zikankhala. Mkwiyo wanga ukugwera pansi pake pomwe. Sindigwiranso mchengawo nthawi yayitali. Mudzalowa m’nyanja kuya kwa kilomita imodzi, mpaka ku Salton Sea. Zidzakhala zoyipa kuposa tsiku lomaliza la Pompeii.

Ndiyeretsa dziko lapansi ndi moto posachedwa. Ndidzaphaya zonse zomwe zili pamwamba pake ndi pansi pake. Mukuona zimene zikuchitika padziko lonse, monga ndinakuuzani. Inu mukuwona Mkwati Wanga akulumikizana pamodzi kuzungulira Mawu Anga, monga Ine ndinakuuzani inu.

Tsopano ndi nthawi. Tsopano ndi nyengo. Dzikonzekereni nokha!

Nthawi la mkwiyo Wake lili pa dziko lapansi. Thawani pamene nthawi ikaliko yothawa, ndi kubwera mwa Khristu.

Inu mukuyitanidwa kuti mubwere kudzalumikizana nafe, gawo la Mkwati Wake, pamene ife tikudzikonzekeretsa tokha Kubwera Kwake, pakumva Liwu la Mulungu likulankhula kwa ife ndi kutibweretsera ife Uthenga: Kusankhidwa Kwa Mkwati 65-0429E Lamlungu lino pa 12:00. P.M., nthawi ya Jeffersonville.

M’Bale. Joseph Branham

Genesis 24:12-14
Yesaya 53:2
Chivumbulutso 21:9

23-0312 Kwawo Kwa Mtsogolo Kwa Mkwati Wa Kumwamba Ndi Mkwatibwi Wa Padziko

Uthenga: 64-0802 Kwawo Kwa Mtsogolo Kwa Mkwati Wa Kumwamba Ndi Mkwatibwi Wa Padziko

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mkwati Wapadziko Lapansi,

Malaki 4 ndi Mawu a Mulungu, ndipo Iwo abala a mtundu wake, IFE, Mkwati Wake. Ndi Mzimu Woyera, Umunthu wa Yesu Khristu, ukugwira ntchito, wokhazikitsidwa mu mitima yathu. Ife timafulumizitsidwa ku Mawu ONSE amene Iye analankhula, pakuti “Nkhosa Zanga zimamva Liwu Langa; mlendo sizimamtsata.”

Mwezi yapita aya yakhala yabwino making, kukonka mneneri mu Jeffersonville. Mulungu wakhala akulankhula kupyolera mwa mngelo Wake wamphamvu ndi kutidyetsa ife ndi Chakudya Chake chosungika kuchokera mu KOLOWE LAKE LIMODZI m’dziko lonselo. Iwo ndi Mana Obisika, niya Mkwati Wake basi.

Ndi Uthenga uliwonse umene timamva, timayanjana ndi kusangalala wina ndi mzake; “Ndikudziwa kuti ndamva Mauthenga awa nthawi zambiri m’mbuyomo, koma SINANDINAYAMBE kumva monga tsopano”. Nizoona ndi kasupe wa Madzi amoyo akutumphukira mkati mwathu. Sitingathe kudziletsa. Ndizo zonse zomwe tikufuna kukambirana. Sitinakhalepo otsimikiza m’miyeo yathu, kuti ndife ndani komanso komwe tikupita.

Palibenso kudabwa:
“Sindikudziwa basi. Ndachita zinthu zambiri zoipa m’moyo wanga. Ndamulephera Ambuye nthawi zambiri. Zikuoneka kuti ndalakwitsa nthawi zonse. ”

Palibenso chiyembekezo:
“Ndikukhulupirira kuti ndine mwana wa Mulungu. NDIKUFUNA kukhala. Ndikupemphera kuti ndine.”

Masiku amenewo ZONSE ZATHA. Tsopano TIKUDZIWA. Ulemerero kwa Mulungu!!

Kodi tikudziwa bwanji? Mulungu wakhala akuyankhula molunjika kwa ife mwa Liwu Lake pa matepi, kutiuza ife mobwereza bwereza, “Ine ndiri mwa inu, inu muli mwa Ine. Ndife AMODZI. Ndinakusankhani inu asanaikidwe maziko a dziko. Inu ndinu mnofu wa mnofu wanga, fupa la Fupa Langa.”

Ndi Uthenga wabwino umene Mulungu analankhula kwa ife Lamlungu kutiuza zonse za mmene dziko limene tikukhalamo siliri lathu, ndi Edeni wa Satana. Momwe iye anamunyenga Eva pachiyambi kuti amufunse ndi kukayika MAWU AMAMODZI. Iye anavula Chophimba Choyera cha Mulungu, ndipo anavala chophimba cha chidziwitso, ndiye maso ake anatseguka ndipo iye anadziwa kuti iye anali wosavala.

Satana anapotoza Mawu apachiyambi, ndipo tsopano wachititsa iye khunkala osaona kuti iye akali wosavala ndipo sakudziwa izo. Iye wakhala mfumukazi ya Satana ndipo dziko lapansili ndi ufumu wake wa Edeni.

Lamlungu, Mkwati wathu wa Kumwamba akufuna kukumbutsa Mkwati Wake wapadziko lapansi kumene Nyumba Yathu Yamtsogolo ili ndi momwe Idzakhalire. “Wokondedwa wokondedwa, tsopano popeza ndakuwuzani zonse za dziko lino ndi momwe liri Edeni wa Satana, ndikufuna ndikuuzeni ANSO za Kwanu Kwamtsogolo ndi Ine.

Ndikufuna ndikuuzeni mwabili vonse. Ndikudziwa kuti mwandimvapo Ine ndikukuuzani za Izo nthawi zambiri, koma yembekezani, nthawi ino zikhala ngati simunanmvepo Ine ndikukuuzani kale.

Ndikufuna kulowa mwatsatanetsatane. Ndikufuna kukuululirani kuti muli mu Chifuniro changa chanbwino pakukhala ndi Mawu Anga ndi mneneri Wanga. Ndikufuna kukupatsani choyimira cha zomwe mukuchita lero ngati mtundu wangwiro wa Mzinda watsopano womwe mudzakhalamo.

Ife ndithudi tilowa mu chinachake. Ine ndikhala ndikugwetsera inu kenakake kakang’ono; Ndikudziwa kuti mudzachigwira Icho. Inu mudzakhala mu Mzinda umenewo ndi Ine. Mneneri wanga adzakhala pafupi ndi inu. adzakhala mnansi wako. Inu mudzayenda m’misewu ya golide iyo ndi kumwa kuchokera ku Kasupe Wanga. Inu mudzakhala mukuyenda kulowa m’paradaiso wa Mulungu, ndi Angelo akugwedezeka ndi kuyimba nyimbo za fuko.

Inu mudzakhala ngale mu korona wa mneneri Wanga. Mudzapambana Chilichonse cha m’dziko Patsiku limenelo. Pali zambiri zomwe ndikufuna kukuwululirani Lamlungu. Ndi tsiku losangalatsa maningi lomwe tidzakhala limodzi”.

Ali ndi zambiri zotisungira masabata angapo akubwerawa, ngati sabwera kudzatitenga nthawiyo isanafike. Sabata ndi sabata, kutiuza ife, yemwe ife tiri, kumene ife tikupita, momwe Izo ziti zidzakhalire Kumeneko. Adzakhala akutitsogolera ku sabata laulemerero la Isitala lomwe takhala nalo, lodzaza ndi china chilichonse koma kumutamanda ndi kupempeza iye.

Ndi nthawi yosangalatsa eyi. Tikuwona uneneri ukukwaniritsidwa pamaso pathu. Ife tikuwona Mawu akuwonetseredwa MWA IFE. Kubwera Kwake kukhoza kukhala nthawi iliyonse. Tiyimirira pakhomo ndi maluwa m’manja mwathu. Timamva mahatchi akuthamanga komanso mchenga ukugwedezeka pansi pa mawilo.

Bokosi lakale liyimitsidwa posachedwa kwambiri. Tidzalumpa mu chitseko cha thupi lakale ili ndikuwulukira mmanja mwake. Iye adzatiyang’ana ife ndi kunena, “Zonse zatha tsopano, wokondedwa, ine ndikutengerani inu tsopano Kwanu Kutsogolo Kwanu.”

Mukuitanidwa kukhala nawo m’masiku opambana kwambiri amene dziko silinaonepo. Mphungu zidzakhala zikusonkhana kuchokera kozungulira dziko kuti zimve Liwu la Mulungu likulankhula kwa Mkwati Wake ndi kumuuza iye zonse za: Kwawo Kwamtsogolo Kwa Mkwati Wa Kumwamba Ndi Mkwati Wapadziko 64-0802, pa 12:00 P.M., nthawi ya Jeffersonville.

M’BALE . Joseph Branham

Chikumbutso: Musaiwale za Nthawi Yosungira Masana.

Malemba oti muwerenge musanamve Uthenga:
Mateyu 19:28
Yohane 14:1-3
Aefeso 1:10
2 Petro 2:5-6 / 3rd Mutu
Chivumbulutso 2:7; 6:14/21:1-14
Levitiko 23:36
Yesaya 4 Mutu 28:10 / 65:17-25
Malaki 3:6

23-0305 Edeni Wa Satana

Uthenga: 65-0829 Edeni Wa Satana

PDF

BranhamTabernacle.org

Ana Anga Okondedwa,

Inu ndimwe chikhumbo cha Ine, Atate anu a Kumwamba. Inu munali mwa Ine kuyambira pachiyambi. Simukukumbukira chabe, koma munali ndi Ine. Ndinafunisisisa kwambiri kukudziwani chifukwa ndimafuna kuti ndikugwireni, kukamba nanu, kumikondani inu, ndi kumiposhani mumanja anu.

Monga mwana wanga, ndiwe gawo la Ine, wopangidwa thupi, monga ine ndinapangidwa thupi, kodi ife tikhoze kukhala ndi chiyanjano wina ndi mzake monga banja la Mulungu pa dziko lapansi. Chimenecho chinali chofuna Changa ndi zomwe ninalikufuna kuchokera pachiyambi.

Ndinakupangirani Munda wa Edeni kuti tiyanjane, koma mdani Wanga anazembera ndi chinyengo, anatenga dziko lapansi ndikutanthauzira molakwika pulogalamu kwa inu.

Iyi ndi nthawi lachinyengo limene mukukhalamo, koma ilinso nthawi yaulemerero kwambiri ya mibadwo yonse, chifukwa tsopano mukuyang’anizana ndi Zakachikwi zazikulu kachiwiri; mukuyang’anizana ndi Edeni kachiwiri.

Mzimu wanga si chinachake chimene chimaphunzitsidwa mwa inu. Ndi chinthu chomwe ine ninakonzedweratu mwa kudziwiratu Kwanga mwa inu ndi kwanja Langa lamphamvu. Tsopano kuitana Kwanga kotsiriza kuli kuti ndimugwire Mkwati Wanga; “chokani pakati pawo, patukani”.

Lero iwo sakuyesera kukhazikitsa Mawu Anga mu mitima ya anthu, iwo ali kuyesera kudzikhazikitsa okha. Mipingo ikuyesera kukhazikitsa chiphunzitso cha mpingo mu mtima wa munthu. Munthu aliyense amati, “Ndachita izi. Ine, ine, changa, chipembedzo changa, ine, ichi.” Akudzikhazikitsa okha, osati Anga Mawu amene analankhulidwa kupitila mwa mneneri wanga.

Inu simukufunika kuti mumvetse chirichonse chimene ine ndikunena, inu muyenera kungokhulupirira Izo chifukwa ine ndinanena chomwecho, ndipo izo zikukhazikitsa icho kwanthawizonse.

Mzimu wanga Woyera ukugwira ntchito mwa inu. Ndi Moyo mwa inu, osati kutengeka; ayi mtundu wina wa umboni wathupi, koma Iwo ndi Munthu, INE, Yesu Khristu, Mawu a Mulungu, okhazikitsidwa mu mtima mwanu, ndipo amafulumizitsa Mawu aliwonse a m’badwo uno. Ndi Mzimu Wanga Woyera ukugwira ntchito mwa inu molingana ndi Mawu.

Mkwati wanga woyamba analephera pakumvetsera kumakanizo ya Satana, koma Ine ndakuwombola iwe mwa Inemwini, amene ali Mawu opangidwa thupi. SIMUDZANDIKANGIWA INU. Inu ndinu Mkwati Wanga wa Mawu namwali amene simudzamvera kumaganizilo ya Satana. Inu mudzakhala ndi Mawu Anga.

Zakachikwi zikadzatha, ndiye padzakhala Edeni wokhazikitsidwa kachiwiri; Ufumu wanga waukulu udzachotsedwa. Ndinalimbana nazo ndi satana m’menemo m’munda wa Getsemane, ndipo ninaiwinaso Edeni Wanga. Tsopano ndapita kuka konza Edeni wanu Watsopano Kumwamba. Ndibweranso kwa inu posachedwa, mitima yanu osati isavutike.

Sipadzakhalanso mumana, pakuti m’mwamba moyamba ndi dziko loyamba zidzapita. ne ndidzayikonzanso iyo ndi ubatizo wa Moto umene uti udzaphe nyongolosi iliyonse, iliyonse matenda, matenda aliwonse, ndi chonyansa chirichonse chimene chinayamba chakhalapo pa dziko lapansi.

Iye adzaphulika, ndipo padzabwera Dziko Latsopano. Kumwamba koyamba ndi dziko lapansi loyamba zidzapita. Padzakhala Yerusalemu Watsopano akugwa kuchokera kwa Ine kuchokera Kumwamba. Kumeneko ndidzakhala ndi inu, makhalidwe Anga azoona, Ana Anga ndi
ana aakazi. Tidzayanjana mu choyera, ndi maso anu kuvalika ku tchimo lililonse.

Ndabweranso kwa inu monga mwamene ndi nakulailani kuti ndidzachita. Ndasunga Yanga Mawu kwa inu. Ine ndakhala nawo Mawu Anga atalembedwa pa tepi ya maginito kuti pasakhale kusamvetsetsana, popanda funso, Mawu anga abwino okha kwa inu; pakuti Iwo uli
Kukamba kwa M’buye.

Khalani ndi mumtima yanu choyera. Sungani mitima yanu yobisika. Yang’anani maso anu ophimbidwa ku zinthu za mdziko kuti akhale winawake wamkulu.

Osayiwala konse, ndidzatembenukira kumadzulo ndikupitamo anso, limodzi la masiku awa. Kufikira pamenepo, tenga Dzina Langa ndi iwe; Izo zidzakusangalatsani ndi kukupatsani inu chitonthozo, zitengeni izo, kulikonse inu komuyenda, pa kutyanka kuliza.

Osanyengerera pa Mawu amodzi. Mawu Anga pa tepi safunika kutanthauzira. Inu ndinu gawo la Ine, chikhumbo Changa. Dzikoli ndi Edeni wa Satana, koma ndakupangani kukhala Edeni Watsopano kumene tidzakhala pamodzi kwamuyaya. Kufikira pamenepo, gwirizanani pa Mawu Anga. Kondanani wina ndi mzake.

Bwerani mujoinane nawo ku Branham Tabernacle Lamlungu lino pa 12:00 P.M., nthawi ya Jeffersonville, ndi kumva Ine ndikuyankhula kupitila mwa mneneri Wanga wosankhidwa ndi kuwulula Mawu Anga pamene inu mukumva; Edeni wa Satana 65-0829. M’malo mwake,

M’bale . Joseph Branham

Malemba oti muwerenge:

2 Timoteyo 3:1-9
Chivumbulutso 3:14
2 Atesalonika 2:1-4
Yesaya 14:12-14
Mateyu 24:24

23-0226 Fyuluta Ya Munthu Woganiza

Uthenga: 65-0822M Fyuluta Ya Munthu Woganiza

PDF

BranhamTabernacle.org

Okondedwa Osonkhana Ndi M’bale Branham,

Ndikufuna kuitana dziko kuti lisakane naife pa kulumikizanitsa Lamlungu lino pa 12:00 P.M., nthawi ya Jeffersonville, pamene ife a chiomba nkanga timasonkhana pamodzi mailosi mazana awiri aliwonse mu umodzi wa mipingo ya mneneri. Tidzamva Mulungu akulankhula kupitira mu mngelo mutumwa Wake wachisanu ndi chiwiri ndi kutiuza kuti:

Uthenga uwu, ndi Mauthenga ena onse amene ine ndimalankhula, walunjikidwa kwa osonkhana anga. Izo si za osonkhana anu koma ngati iwo akufuna kuti achilandire Icho. Koma Izo zalunjikidwa kwa anthu awa pano.

Iye akulankhula kwa ife, ULEMERERO, osonkhana ake. Osati inu amene mumati, “M’bale Branham ndi mneneri, koma iye si m’busa wanga. Abusa athu akuti kuliza matepi mu tchalitchi simolingana ndi Mawu amasiku ano.” “M’busa wathu amatiuza kuti tizimumvera. Molingana ndi Mawu, akutitsogolera ndi Mzimu Woyera tsopano.”

Mneneri anakulankhulani inu ndi abusa anu.

Kwa atumiki aliwonse pa malo aliwonse, nthawi iliyonse, izi sizinalunjikidwe monyozera ku ziphunzitso zanu, izi sizinalunjikidwe nkomwe kwa nkhosa zanu.

Sitifuna kukangana nanu abale ndi alongo. Ife tikumvetsa, Izo sizinalunjikidwe kwa inu, koma kwa ife, amene timakhulupirira kuti Mzimu Woyera wayika mngelo Wake wachisanu ndi chiwiri mutumiki kuti akhale m’busa wathu ndi kutitsogolera ife, mpingo Wake. Ife timakhulupirira kuti kuliza matepi ndi NJIRA YAZOONA YOKHA. Mulichabebwino ndipo mukuchita zomwe mneneri wakuuzani kuti muchite:

Ndipo ine nthawizonse ndimalozera kwa iwo, ngati iwo ali membala wa mpingo wina, “Kawoneni abusa anu.”

Muyenera kuchita monga momwe abusa anu akunenera.

Kenako mneneri amauza abusa anu, kuti atsimikize kuti amvetsetse.

Tsopano, abusa, ine ndikufuna inu mudziwe izo, kuti, izi ndi kwa osonkhana anga okha omwe ine ndimalankhula zinthu izi. Ndipo ine ndiri nawo ufulo wochita zimenezo, chifukwa ine ndinaikidwa ndi Mzimu Woyera kuti ndiziyang’anira nkhosa izi.

Watumidwa kuti aziyang’anira ife, nkhosa zake; amene Mulungu wawaika mu zisamaliro AKE. Mzimu Woyera ndi m’busa wathu pamene Iye akulankhula kwa ife ndi kutitsogolera ife tsiku lirilonse ndi Liwu Lake lotsimikiziridwa.

Izi ndi zimene Yehova akutitsogolera kuchita. Ife sitikutsutsa inu kapena abusa anu, kapena momwe inu mukumverera kutsogozedwa ndi Ambuye kuti muchite. Munthu aliyense ayenera kuchita zimene akuona kuti Yehova akumutsogolera kuchita mogwirizana ndi Mawu.

Tili ndi chosefela chimodzi, UTHENGA UWU. Chirichonse chimene timamva chiyenera kupita mu sefa imeneyo. Liwu limene timamva pa matepi ndilo Liwu lokha lomwe tili nalo 100% kukutila kuti NDI KULANKULA KWA AMBUYE.

Kodi inu mukhulupirira kuti kudzoza kumeneko pa anthu amenewo kutanthauza kuti ndi kudzoza kwa Mzimu Woyera?” Inde, bwana, Mzimu Woyera weniweni wa Mulungu pa munthu, koma iwo ndi abodza.

Kopita kwathu Kwamuyaya zimatengera zomwe IYE ANENA PATEPI, osati zomwe munthu wina aliyense kapena gulu la anthu likunena. Choncho, sitingathe, ndipo sitidzamva wina aliyense. Kodi munthu angachite bwanji mwayi?

Bwerani mudzasonkhane pamodzi ndi ife mochulukira, popeza muona kuti tsiku lilikuyandikira.

Anthu akhoza kukhala mnyumba zawo momwemo kapena mwawo…kusonkhana m’malo awo, matchalitchi awo, ndi zina zotero, ndi kumvetsera misonkhano.

Kuti, abwenzi anga, molingana ndi mneneri wa Mulungu, osati kutanthauzira kwa munthu wina pa zomwe Baibulo limanena, tikudzisonkhanitsa tokha pamodzi mozungulira Mawu mochuluka kwambiri momwe ife tikuwonera tsiku likuyandikira.

Kodi chingalawa popanda Mulungu n’chabwino bwanji? Ndi bokosi yankuni chabe, magome angapo amiyala.

Bwerani mudzasonkhane nafe pamene tikumvera chosefela choperekedwa ndi Mulungu, pamene akutibweretsera Uthenga: Chosefela Cha Munthu Woganiza 65-0822E.

M’bale. Joseph Branham

Onani zomwe mukumenyera. Onani zomwe mulili pano. Yang’anani zomwe mumapitira kutchalitchi. Zomwe zimakupangitsani inu…Ndi zabwino kupita ku tchalitchi, koma osanpita ku tchalitchi kokha; izo sizingakupulumutseni inu.

23-0219 Khristu Akuwululidwa Mu Mawu Ake Omwe

Uthenga: 65-0822M Khristu Akuwululidwa Mu Mawu Ake Omwe

PDF

BranhamTabernacle.org

Nkhosa zanga zazing’ono,

Moni kwa inu ndi inu pama foni awa, zabwino kwambiri.Ndine wothokoza kwambiri kwa Ambuye inu mukhoza kukhala mnyumba mwanu momwe, kusonkhana mu malo anu, mipingo yanu, ndi kumva bulaliki. Kulikonse kumene liwu langa likubwera, lekani gulu laling’ono ilo lidalitsidwe.

Lero, ndikufuna kukulemberani kalata yachikondi yochokera pansi pamtima kuti ndikulimbikitseni. Inu ndinu amene Mulungu anasankha kuti mukhale Mkwati Wake kuchokela kuchiyambi cha dziko; inu mukumvera matepi aya. Ine ndikuuzani inu nthawi zambiri, matepi aya ndi anu okha, ndinu osonkhana anga. Ine ndiribe udindo pa zomwe Mulungu anapatsa atumiki ena kuti azidyese; Ndili ndi udindo pa mtundu wa Chakudya chomwe ndimakupatsirani. Matepi aya ndi a inu, mpingo wanga yekha, amene Mulungu wandipatsa kukala mbusa. Ndi Manna obisika, winayo sangakhoze kutenga Izo.

Tsopano, ngati anthu ena akufuna kupanga haibridi chakudya ndi zinthu kunja uko, asiyeni iwo atenge vumbulutso kuchokera kwa Mulungu ndi kuchita zomwe Mulungu akuwauza iwo kuti azichita, azidya pa chirichonse chimene iwo akufuna. Ndichita zomwezo. Koma Mauthenga awa nkwa inu nokha.

Ine ndikuyesera mwakukhoza kwanga kukhala ndi Mawu, kwa inu amene mwayikidwa mmanja mwanga kuchokera kwa Mulungu, chifukwa nkhosa zimafuna chakudya cha nkhosa. “Nkhosa Zanga zimamva Liwu Langa.” Ndipo ndicho chimene ife timakhalira moyo, Mawu aliwonse amene atuluka. Osati Mawu chabe nthawi ndi nthawi, koma Mawu aliwonse amene atuluka kuchokera mkamwa mwa Mulungu. Ndi chimene inu oyera mtima mumakhala nayho.

Aliyense ayenera kukhala ndi chinachake chimene angagwire .Chinachake chiyenera kukhala chomangirira, mwa kuyankhula kwina, chodalirapo. Ndipo aliyense ayenera kukhala nacho mtheradi kapena mtheradi. Kwa ine, ndi kwa iwo amene ine ndikuyembekeza kuti ine ndikuwatsogolera kwa Khristu, ndi mwa Khristu, Baibulo ndilo chochidalira chathu.

Tsopano, ife tikuzindikira kuti Mulungu anatitumizira ife aneneri Ake. Umo ndi momwe Iye aliri ndi kubweretsa Mawu Ake kwa anthu, kupitila mu milomo ya mneneri Wake. Tsopano mu masiku otsiriza ano, Iye walonjeza kuti adzadziwonetsera Yekha mu chidzalo kachiwiri, cha thupi Lake, mu Mzimu. Ndi Mulungu Mwiniwake mu mawonekedwe a chilembo, mawonekedwe a mneneri, akuwonetseredwa mu thupi.

Ine ndiyenera kukhala lyonse mu Kukhalapo kwa analemba ndi cholembera changa chokonzeka nthawi iliyonse kuti nilembe chirichonse chimene Iye anena. Ine ndimayika maganizo anga pa maganizo Ake; osati zomwe munthu amaganiza, zomwe m’badwo ukuganiza, zomwe mpingo ukuganiza, zomwe ufumu ukuganiza. Maganizo a Mulungu okha! Ndimangofotokoza maganizo a Mulungu ku Mawu.

Pamene Mulungu awulula maganizo Ake kwa ine, ine ndimazifotokoza izo mu Mawu kwa inu pa tepi, “KUKAMBA KWA AMBUYE.” Izo siziri, “Kukamba kwa ine.” Ndi, “KUKAMBA KWA AMBUYE!” Ine ndingakhoze kokha kuwatanthauzira Iwo monga Analemba anivomeleza ine kuti ndikutanthauzire kwa inu; pakuti Iwo ali Mawu osalephera a Mulungu.

Alipo ena ambiri amene amayesa kunikopela ine, monga ansembe, ndi zina zotero. Ndipo amachita chiyani? Ingosokonezani, ndizo zonse. Iwo sakhoza kuchita izo. Mulungu anandituma ine, mneneri Wake, kuti ndidzamutsogolere Mkwati Wake; osati munthu wina, kapena osati gulu la amuna.

Mawu omwe ndikunena, ndi momwe ndimachitira, adzachititsa khusaona ena, koma adzatsegula maso a ena. Iye anandivalika ine mu mtundu wa diresi limene ine ndifunika ndivale, chikhalidwe changa, chikhumbo changa, chirichonse basi momwe ine ndiyenera kukhalira. Anakusankhirani ine mwabwino. Ena amaima ndi kuyang’ana ndi kunena, “Chabwino, sindingathe. Pali…ine—ine sindikukhoza kuwona.” Iwo achititsidwa khusaona.

Adzaulula kwa amene Iye adzaulula. Iye anapangidwa kotero kuti Iye akhoza kudzibisa Yekha mu Lemba, kwa wazamulungu wochenjera kwambiri amene alipo. Iye akhoza kungodzibisa Yekha, kukhala apo pomwe mu Lemba, ndipo iwo akhoza kuyang’ana utali wa tsiku lonse ndipo osachiwona icho; kuyang’anani moyo wonse, ndipo osachiwona icho. Iye akhoza kungodzibisa Yekha, kunkhala pamenepo.

Chofunikira tsopano ndi iwo amene alandira Uthenga mu mitima yawo, ayenera kunkala mu Kukhalapo kwa Mwana, kuti akachepe. Lisani matepi ndiyeno lolani Mwana aphike zobiriwira zonse mwa inu, kukupangani inu Akhristu okhwana.

Pamene iye anabwera nthawi yoyamba, iye anali munthu. Pamene iye anabwera nthawi yachiwiri; ndi magawo awiri, iye anali munthu. Pamene iye anabwera mu mawonekedwe a Yohane M’batizi, iye anali munthu. Iye analonjeza kubwera tsiku lino ndi kukhala moyo ndi kudziulula Yekha kamodzinso mwa munthu; Mwana wa munthu akukhala m’thupi la munthu.

Ife tsopano tiri mu m’badwo wa Maso, aulosi, wa Malaki 4. Palibe china chatsalira kuti icho chibwere koma Iye Mwiniwake kuti alowe mu zimenezo, ’chifukwa ndicho chinthu chotsiriza chimene chiripo.

Mvetserani ana ankhosa anga, inu amene Mulungu wandipatsa ine kwa m’busa. Nthawi lachedwa. Iye azabwela posachedwa, Mkwati Wake. Khalani nawo matepi amenewo, ayo siyafunika kutanthauzira.

Ine ndikukuitanani inu a Mphungu aang’ono kuti mubwere mudzalumikizana nane ndi chinthu chokha chimene chidzabweretse Mkwati Wake pamodzi Lamlungu lino, pa 12:00 p.M., nthawi ya Jeffersonville. Mudzamva Kukamba kwa Ambuye pamene Mulungu akulankhula kupyolera mwa ine ndi kuwulula: Khristu Akuwululidwa Mmawu Ake 65-0822M.

Kumbukirani, KHALANI NDI UTUMIKI WA TEPI.LISANI MATEPI TSIKU LONSE.

M’bale Branham

Malemba o werenga pamene mukalibe kumva Uthenga:

Eksodo 4:10-12
Yesaya 53:1-5
Yeremiya 1:4-9
Malaki 4:5
Luka 17:30 St
Yohane Woyera 1:1 / 1:14 / 7:1-3 / 14:12 / 15:24 / 16:13
Agalatiya 1:8
2 Timoteyo 3:16-17
Ahebri 1:1-3 / 4:12 / 13:8
2 Petulo 1:20-21
Chivumbulutso 1:1-3 / 10:1-7 / 22:18-19