Uthenga: 63-1229M Pali Munthu Pano Yemwe Akhoza Kuyatsa Kuwala
Category Archives: Uncategorized
25-1012 Kusimidwa
Uthenga: 63-0901E Kusimidwa
Wokondedwa Mkwatibwi wa Tepi,
Tsopano inu anthu mu matepi kumeneko.
Ambuye, ife tingayambe bwanji kufotokoza chimene mawu aang’ono asanu ndi limodzi awa akutanthauza kwa ife, Mkwatibwi wa Yesu Khristu? Ndi Vumbulutso la Uthenga wa orali kwa ife. Ndi Mulungu akuyankhula kupyolera mwa m’thenga Wake wa mngelo kumuuza Mkwatibwi Wake, “Ine ndikudziwa inu mudzakhala ndi Liwu Langa. Ine ndikudziwa chimene Mawu Anga pa matepi awa ati adzatanthauze kwa inu.Ine ndikudziwa inu mudzakhala ndi Vumbulutso kuti Mauthenga awa amene ine ndawayankhula mu matepi ali Chizindikiro Changa cha lero.”
“Ine ndaika Liwu Langa pa matepi a maginito awa; pakuti Mauthenga awa ayenera kutsirizitsa Mawu onse. Padzakhala zikwi kuchulukitsa zikwi amene ati adzamve Liwu Langa pa matepi ndipo adzakhala ndi Vumbulutso kuti uwu ndi utumiki Wanga.Ndi mzimu woyera wa lero. Ndi uthenga wanga wa chizindikiro
“Ine ndatumiza atumiki okhulupirika ambiri ku dziko lonse lapansi kuti akalengeze utumiki Wanga. Pamene iwo anabwerera, iwo anandiuza Ine, ‘Ife tamvera malamulo Anu mwa kusewera matepi Anu.Ife tinapeza anthu amene amakhulupirira Mawu aliwonse. Iwo apanga nyumba za Iwo eni kukhala tchalitchi zolandiliramo Uthenga Wanu. Ife tinawauza iwo, onse amene akanadzabwera pansi pa Chizindikiro Chanu, Uthenga wa orali, akanadzapulumutsidwa.’”
Ndi nthawi yomwe munthu aliyense ayenera kudzifufuza ndikudzifunsa yekha, kodi njira yangwiro ya Mulungu lero ino ndi iti? Mawu a mneneri sanalepherepo nthawi imodzi. Icho chatsimikiziridwa kuti ndi Choonadi CHOKHA, CHINTHU CHOKHAKO chimene chiti chidzamuyanjanitse Mkwatibwi Wake.
Chirichonse chimene iye ananena chachitika ndendende basi momwe iye ananenera icho. Lawi la Moto likadali pano ndi ife.Liwu la Mulungu akuyankhulabe ndi ife pa matepi. Mneneri anangotiuza ife kuti Mulungu analambala pamwamba kokha pamene Iye adawona Chizindikiro. Ndi nthawi ya kusimidwa kuti onse alowe pansi pa Uthenga wa Chizindikiro uwo.
Ife taliwona Dzanja lamphavu la Mulungu mu nthawi yotsiriza ino. Iye watipatsa ife Vumbulutso loona la Mawu Ake ndipo ilo labwera pansi pa chisonyezo cha Chizindikiro. Tsopano, pamene ife tiri pansi pa chisonyezo cha Chizindikiro, tiyeni ife tibwere palimodzi ndi kudya Mgonero mwa kusimidwa; pakuti tidziwa kuti Mulungu akukozekera kuti akanthe ndi chiweruzo.
Ndikufuna kuitana aliyense wa inu kuti mumve ndi kukhala ndi M’gonero ndi Utumiki wosambitsana Mapazi Lamlungu lino, pamene tikumva Uthenga: Kusimidwa 63-0901E.
Uthenga ndi utumiki wa Mgonero udzakhala pa Wailesi Ya Liwu kuyambira 5:00 P.M. nthawi ya ku Jeffersonville . Chonde khalani omasuka kukhala ndi chiyanjano chanu nthawi ya kwanuko ngati mungafune, monga ndikudziwira kuti zidzapangitsa kukhala kovuta kwa okhulupirira athu ambiri akunja kuyamba chiyanjano chawo panthawiyo. Padzakhala ulalo wa fayilo yotsitsika ya utumiki.
M’bale. Joseph Branham
Malemba oti muwerenge musanayambe chiyanjano:
Ekisodo 12:11
Yeremiya 29:10-14
Luka 16:16 St
Yohane 14:23
Agalatiya 5:6
Yakobo 5:16
25-1005 Chizindikiro
Uthenga: 63-0901M Chizindikiro
- 25-1005 Chizindikiro
- 23-1217 Chizindikiro
- 22-0605 Chizindikiro
- 21-1219 Chizindikiro
- 20-0315 Chizindikiro
- 19-0825 Chizindikiro
- 17-0820 Chizindikiro
Wokondedwa Mkwatibwi Wa Chizindikiro
Pamene ife tibwera palimodzi, ife sitimangoyankhula za Uthenga, ife timabwera palimodzi kuti tidzaike Magazi, kuti tiike Chizindikiro; ndipo Chizindikiro ndi Uthenga wa orali! Ndiwo Uthenga wa tsiku lino! Ndiwo Uthenga wa nthawi ino.
Ife tayika Chizindikiro icho kwa ife eni, ku nyumba zathu, ndi kwa mabanja athu. Sitikuchita manyazi. Sitisamala amene akudziwa. Tikufuna kuti aliyense adziwe, wodutsa aliyense awone ndi kudziwa: Ndife Anthu a atepi. Ndife a Tepi yapa nyumba . Ndife Mkwatibwi wa Tepi wa Mulungu.
Mzimu Woyera = Chizindikiro = Uthenga. Onse ali ofanana. Simungathe kuwalekanitsa. Atate, Mwana, Mzimu Woyera = Ambuye Yesu Khristu. Simungathe kuwalekanitsa. Uthenga = Mtumiki. Ziribe kanthu zomwe otsutsa anena, M’NENERI ANATI, inu simungakhoze kuwalekanitsa iwo.
Mulungu ndiye chimwemwe chanu. Mulungu ndiye mphamvu yanu. Kudziwa Uthenga uwu, kudziwa kuti Iwo ndi Choonadi chokha, kudziwa kuti Icho ndi Chizindikiro, ndiko kukwanira kwathu. Ena akhoza kunena, “Ine ndimawakhulupirira Iwo, ine ndimawakhulupirira Iwo, ine ndikukhulupirira Iwo ndi Choonadi. Izo zonse nzabwino, komabe Izo ziyenera kuyikidwa.
Mneneri anati Uthenga uwu ndi Chizindikiro cha lero. Uthenga uwu ndi Mzimu Woyera. Ngati inu muli ndi Vumbulutso lirilonse la Uthenga uwu inu mukhoza kuwona momveka ora limene ife tikukhalamoli. Ochuluka kwambiri akunena, “Ine ndikukhulupirira Iwo. Mulungu anatumiza mneneri. Iwo uli Uthenga wa ora,” koma Iwo amadzitama ponena kuti iwo satero, ndipo sadzatero, kusewera Liwu lomwe la Chizindikiro mu mipingo yawo.
Mulungu sanalankhule kupyolera mwa mngelo Wake wamphamvu ndi kungonena chinachake pokhapokha ngati chinali ndi tanthauzo. Iye anatiuza ife kuti anatiphunzitsa ife mwa zoimira ndi mithunzi. Mu Uthenga uwu, mneneriyu akufotokoza mwatsatanetsatane kutiuza zimene Rahabi ndi a banja lake anachita kuti apulumutsidwe, kuti akhale Mkwatibwi. Anafotoza momveka bwino pa zomwe mkaziyo anachita.
Pamene anyamata a tepi ankasewera “TEPI”…Dikirani miniti, kodi mthenga uja anachita chiyani? Anasewera Tepi. Ndiye kodi iye anachita chiyani? Anayipanga iye nyumba yake MPINGO WA TEPI. Iye sanachite manyazi kunena kuti, “Onani chingwe chofiyira icho, izo zikutanthauza kuti ine ndine wa MPINGO WA TEPI”.
Inu mukuganiza ngati iye akanati, “Inde, ine ndikumukhulupirira m’thenga ndi Uthenga, koma ife sitimaseweranso Matepi ndipang’ono pomwe mu mpingo wathu. Ndili ndi m’busa amene amati AYI, iyeyo ayenera kungolalikira ndi kubwereza zomwe matepi amanena.” Inu mukuganiza kuti mkazi uja akanapulumutsidwa…???
Iye anaika chizindikiro, ndipo nyumba yake inapulumutsidwa, kapena iye akanawonongeka kumusi uko komwe iye anali.
Mwamvapo atumiki ambiri akupereka zifukwa zodzikhululukira ponena za kusewera matepiwo, koma ambiri a iwo amati: “Mneneri sananenepo kuti azisewera matepiwo m’tchalitchi.”
Mneneri anati Rahabu anayipanga iye nyumba yake kukhala tchalitchi, ndipo mpingo wake unkasewera Matepiwo. Ndipo chifukwa chakuti iye ankasewera Matepi mu mpingo wake, iye, ndi Mpingo wake wonse wa TEPI, anali pansi pa Chizindikiro ndipo anapulumutsidwa. Mpingo wina uliwonse unawonongeka.
Abale ndi alongo, chonde, ine sindikunena kuti m’busa sangakhoze kulalikira Uthenga uwu, kapena kuti ndi zolakwika ngati iye atero. Mwa njira yanga yanga, Ine ndikulalikira tsopano kupyolera mu kalata iyi, koma tsegulani mtima wanu ndi kumvetsera zimene mneneri akunena ndi kukuchenjezani inu. Ngati m’busa wanu akukana, kapena adzakana, kuti azisewera matepi mu mpingo wanu pakupanga chowiringula cha mtundu wina; chirichonse chimene chingakhoze kukhala ziribe kanthu kuchuluka kwa zomwe iye anena “Ine ndikukhulupirira Uthenga wa orali,” molingana ndi zomwe ine ndikukhulupirira Mawu akunena, Chizindikiro, Uthenga wa orali, iwo sukuyikidwa.
Lamlungu lino, ine ndikukuitanani inu kuti mubwere mudzamvetsere ndi Branham Tabernacle pa 12:00 p.M., nthawi ya ku Jeffersonville, ku Uthenga: Chizindikiro 63-0901M. Ngati inu simungakhoze kutijowina ife, sewerani Uthenga wa Chizindikiro uliwonse, ndi kuwuyika Iwo.
M’bale. Joseph Branham
Malemba oti muwerenge musanamve Uthenga:
Genesis 4:10
Ekisodo chaputala 12
Yoswa mutu 12
Machitidwe 16:31/19:1-7
Aroma 8:1
1 Akorinto 12:13
Aefeso 2:12/4:30
Ahebri 6:4 / 9:11-14 / 10:26-29 / 11:37 / 12:24 / 13:8, 10-20
Yohane 14:12
25-0928 Nthawi Yolumikizana Ndinso Chizindikiro
Uthenga: 63-0818 Nthawi Yolumikizana Ndinso Chizindikiro
- 25-0928 Nthawi Yolumikizana Ndinso Chizindikiro
- 23-1126 Nthawi Yolumikizana Ndinso Chizindikiro
- 22-0515 Nthawi Yolumikizana Ndinso Chizindikiro
- 19-0811 Nthawi Yolumikizana Ndinso Chizindikiro
- 17-0702 Nthawi Yolumikizana Ndinso Chizindikiro
- 15-0909 Nthawi Yolumikizana Ndinso Chizindikiro
Wokondedwa Mkwatibwi Wolumikizitsidwa,
Ndine wokondwa kwambiri, ndipo pansi pa chiyembekezero chachikulu chotero, kukhala gawo la zonse zomwe Mulungu akuchita mu tsiku lathu. Malingaliro a Mulungu pachiyambi tsopano akukwaniritsidwa pamaso pathu, ndipo ife ndife gawo la icho.
M’Baibulo lonse, aneneri analosera ndi kunena zimene zikanadzachitika. Nthawizina mauneneri amenewo sanakwaniritsidwe kwa mazana a zaka kenako, koma pamene chidzalo cha nthawi chinadza, icho chinafika pochitika; pakuti ganizo la Mulungu loyankhulidwa mwa mneneri wake liyenera kuchitika.
Mneneri Yesaya anati, “namwali adzaima.” Banja lililonse la Aheberi linakonzekeretsa mwana wawo wamkazi kuti abereke mwana. Iwo anagula izo nsapato ndi nsapato, ndi Birdseye wamng’ono, ndipo anakonzekera kuti mwanayo abwere. Mibadwo inapita, koma potsiriza Mawu a Mulungu anakwaniritsidwa.
Monga kamnyamata ine kakukula nthawizonse ndimadabwa, Ambuye, ine ndikuwona mu Mau anu kuti nthawi zonse mumagwirizanitsa anthu anu pamodzi kuti akwaniritse mawu anu. Munagwirizanitsa ana Anu Achihebri pamodzi mwa munthu mmodzi, Mose, amene anawatsogolera iwo ndi Lawi la Moto kupita ku Dziko Lolonjezedwa.
Pamene Inu munakhala thupi ndi kukhala pa dziko lapansi, Inu munagwirizanitsa ophunzira Anu. Inu munawalekanitsa iwo ku chirichonse ndi aliyense kuti awulule Mawu Anu kwa iwo. Pa tsiku la Pentekosite, munasonkhanitsanso Mpingo Wanu palimodzi pa malo amodzi, mu malingaliro amodzi ndi mtima umodzi musanabwere ndi kuwapatsa iwo Mzimu Woyera.
Ndinaganiza, zingatheke bwanji lero Ambuye? Mkwatibwi wanu wamwazikana padziko lonse lapansi. Kodi Mkwatibwi yense adzabwera ku Jeffersonville? Sindikuwona zomwe zikuchitika Ambuye. Koma Ambuye, Inu simumasintha dongosolo Lanu. Ndi Lamulo Lanu, palibe njira yoletsera. Inu muzichita motani izo?
ULEMERERO…LERO, tikhoza kuona ndi maso athu, ndipo koposa zonse, KHALANI GAWO LA ICHO: Mawu Amuyaya a Mulungu akukwaniritsidwa. Sitili MWATHUPI pamalo amodzi, tafalikira padziko lonse lapansi, koma Mzimu Woyera TSOPANO WALUMIKIZANITSA MKWATIBWI WAKE NDI MAWU A MULUNGU. MAWU AKE ANALANKHULIDWA NDIPO ANAJAMBULIDWA PA MATEPI, Mtheradi wa Mulungu wa lero, ukusonkhanitsa ndi KULUMIKIZANITSA MKWATIBWI WAKE… NDIPO PALIBE CHINACHILICHONSE CHINGAYIMITSE ICHO.
Mulungu akulumikizitsa Mkwatibwi Wake. Iye akubwera pamodzi, kuchokera Kummawa ndi Kumadzulo, ndi Kumpoto ndi Kummwera. Pali nthawi yolumikizana, ndipo iyo ikuchitika pakali pano. Kodi Iye akulumikizanira chiyani? Mkwatulo. Amen!
Nthawi yolumikizana ikuchitika PANO!!! Kodi chikutigwirizanitsa ndi chiyani? Mzimu Woyera mwa Mawu Ake, Liwu Lake. Kodi tikugwirizanitsa chiyani? MKWATULO!!! Ndipo tonse tikupita ndipo sitikusiya MMODZI kumbuyo.
Mulungu akumukonzekeretsa Iye. Inde bwana, kulumikizana! Kodi Iye akulumikizana ndi chiyani? Ndi Mawu!
Kodi Mawu amasiku ano ndi chiyani? UTHENGA uwu, MAWU AKE, Liwu la Mulungu kwa Mkwatibwi Wake. Osati mwamuna. Osati amuna. Osati gulu. Otsimikiziridwa, ndi Lawi la Moto, MAWU a Mulungu pa matepi.
“Pakuti miyamba yonse ndi dziko lapansi zidzapita, koma Mawu Anga sadzapita.” Iye akudzilumikizitsa Iyemwini ndi PAKUTI ATERO AMBUYE mosalabadila zimene chipembedzo chirichonse kapena wina aliyenseyo akunena.
Mosasamala chimene ALIYENSE anena, ife tikulumikizana ndi zotsimikiziridwa, zotsimikiziridwa, Atero Liwu la Ambuye la tsiku lathu. Osati kutanthauzira kwa wina; tingachite bwanji zimenezo? Izo zimasintha ndi munthu aliyense, koma Liwu la Mulungu pa matepi SALISINTHA ndipo Ilo lalengezedwa ndi Lawi la Moto Lokha kuti ndi Mawu a Mulungu ndi Liwu la Mulungu.
Vuto lake ndi lakuti, ndi munthu, iye samamudziwa mtsogoleri wake. Inde, bwana. Iwo amasonkhanira chipembedzo, iwo amamusonkhanira bishopu kapena munthu, koma iwo sangamusonkhanire Mtsogoleri, Mzimu Woyera mu Mawu. Mukuona? Iwo amati, “O, chabwino, ine ndikuwopa ine ndikhala wotengeka pang’ono; ine ndikuwopa ine ndiponda phazi lolakwika.” Ohhhh, ndi zimenezotu!
Apa ndi pamene otsutsa amalozera kwa mipingo yawo ndi kuti, “Onani, iwo akukwezera mmwamba munthu, M’bale Branham.
Zachabechabe, tikulumikizana mozungulira MAWU OYENZEDWA A MULUNGU OLANKHULIDWA KUPYOLERA MUNTHU UYO. Kumbukirani, ameneyo ndi mwamuna yemwe Mulungu anamusankha kuti akhale Liwu Lake kuti aitane ndi kutsogolera Mkwatibwi Wake mu tsiku lino. Limenelo ndi Liwu LOKHALA lotsimikiziridwa ndi Mulungu Mwiniwake.
Koma mophonya , IWO akulumikizana mozungulira ANTHU. Iwo sakusewera Liwu la Mulungu pa matepi mu mipingo yawo. Kodi inu mungaganize moteromo??? Mtumiki amene amadzinenera kuti akukhulupirira Uthenga uwu kuti ndi Uthenga wa nthawi ino, pakuti Atero Ambuye, koma akupeza chowiringula chamtundu wina choti SANGAKHOZE kusewera Liwu limenelo mu mipingo yawo, koma azitumikira kwa anthu iwo AYENERA kumvetsera kwa iwo ndi atumiki ena akulalikira Mawu… ndiye amati ife tikutsatira munthu!!!
Tangomva Lamulungu lapitali zomwe Mulungu anawachitira amuna amenewo!!
Tikukonzekera Ukwati. Ife tikukhala Mmodzi ndi Iye. Mawu amakhala inu, ndipo inu mumakhala Mawu. Yesu anati, “Pa tsiku limenelo inu mudzadziwa izo. Onse Atate ali, Ine ndine; ndipo zonse Ine ndiri, inu muli; ndipo nonse inu muli, Ine ndiri. Mu tsiku limenelo inu mudzadziwa kuti Ine ndiri mwa Atate, Atate mwa Ine, Ine mwa inu, ndi inu mwa Ine.”
Zikomo Ambuye chifukwa cha Vumbulutso la Inu Nokha, ndi ifeeni, mu tsiku lathu. Mkwatibwi Wanu podzikonzekeretsa Yekha ndi Mawu Anu Olankhulidwa. Tikudziwa kuti tili mu Chifuniro Chanu changwiro pakukhala ndi Mawu Anu olembedwa.
Ndikuitana dziko kuti limvetsere ku Liwu lokhalo lotsimikiziridwa la Mulungu la tsiku lathu Lamulungu lino. Muli wolandiridwa kulumikizana nafe Lamulungu nthawi ya 12:00 p.m., nthawi ya ku Jeffersonville, pomwe tikumvera: 63-0818, Nthawi Yolumikizana Ndinso Chizindikiro . Ngati simungathe kulumikizana ndi kumvetsera nafe, sankhani tepi, TEPI ILIYONSE; iwo onse ali pakuti Atero Ambuye, ndipo mvetserani ku Mawu a Mulungu kukupangani inu kukhala angwiro ndi kukupangani inu kukonzekera kubwera Kwake posachedwa.
M’bale. Joseph Branham
Masalimo 86:1-11
Mateyu 16:1-3
Iye akudzilumikizitsa Iyemwini. Iye akukonzekera. Chifukwa chiyani? Iye ndi Mkwatibwi. Uko nkulondola. Ndipo Iye akudzilumikizitsa Iyemwini ndi Mkwati Wake, mwaona, ndipo Mkwati ndi Mawu. “Pachiyambi panali Mawu, Mawu anali ndi Mulungu, ndipo Mawu anali Mulungu. Ndipo Mawu anasandulika thupi ndipo anadzakhala pakati pathu.”
25-0921 Chitsutso
Uthenga: 63-0707M Chitsutso
Okondedwa Iwo Omasulidwa,
Tsopano, kumeneko, “iwo,” osati wochimwa. “Iwo,” amenewo ndi, mpingo wa tsiku limenelo, iwo anapeza cholakwika ndi Munthu Yemwe anali Mawu. Ndi kulondola uko? Iwo anapeza cholakwika ndi Munthu Yemwe anali Mawu. Tsopano iwo akupeza cholakwika ndi Mawu akugwira ntchito kupyolera mwa munthu.
Kuyambira pachiyambi dziko lamukana Iye, linamukana Iye, linakana kukhala ndi Mawu Ake pa kusunga ndi miyambo yawo, zikhulupiriro zawo, malingaliro awo. Iwo nthawizonse amaphonya dongosolo la Mulungu; Mulungu, monga Munthu, yemwe anali Mawu, ndipo tsopano Mawu akugwira ntchito kupyolera mwa munthu.
Koma mu tsiku lathu Iye anati, “Ine ndidzakhala nawo gulu laling’ono, osankhidwa apang’ono, iwo anali mwa Ine kuchokera pachiyambi. Iwo adzandilandila Ine ndi kudzakhulupilira mau anga ndi Munthu yemwe Ine ndinamusankha kudzaulula mau anga. Iye adzakhala Liwu Langa kwa iwo
“Iwo sadzachita manyazi kulalikira Liwu Langa.” Iwo sadzachita manyazi kuuza dziko kuti Ine ndabwera kachiwiri ndipo ndadziwonetsera Ndekha kupyolera mu thupi la munthu monga Ine ndinanenera kuti Ine ndidzachita. Nthawi imeneyi iwo sadzamupembedza munthuyo, koma iwo azidzandipembedza Ine, Mawu, amene ati adzayankhule kupyolera mwa munthu. Adzandikonda Ine ndi kundilengeza mu m’tsempha uliwonse wa umunthu wawo.”
“Potero, Ine ndawapatsa iwo zonse zomwe iwo akusowa kuti akhale Mkwatibwi Wanga. Ine ndawalimbitsa iwo ndi Mawu Anga; pakuti iwo ALI MAWU ANGA atasandulika thupi. Ngati iwo akusowa machiritso, iwo alankhule Mawu Anga. Ngati iwo ali ndi chotchinga chirichonse chimene chimawatchinga iwo, iwo alankhule Mawu Anga. Ngati iwo ali ndi mwana yemwe walowelela, iwo alankhule Mawu Anga. Chirichonse chimene iwo akusowa, iwo alankhule Mawu Anga, pakuti iwo ali Mawu Anga opangidwa thupi mwa iwo.”
“Iwo akudziwa omwe iwo ali, pakuti Ine ndadziululira Inemwini kwa iwo. Iwo akhala owona ndi okhulupirika ku Mawu Anga ndipo akulumikizana palimodzi kuzungulira Liwu Langa.Pakuti iwo akudziwa Liwu Langa, Mawu Anga, Mzimu Wanga Woyera. Iwo akudziwa, kumene kuli Mawu, Mphungu zidzasonkhanitsidwa.”
Pamene mneneri Wake akulankhula Mawu Ake ndi kuwutsutsa m’badwo uno wa kumupachika Yesu Khristu kachiwiri ndi kulengeza kuti iwo awonongedwa, Mkwatibwi adzakhala akusangalala. Pakuti ife tikudziwa IFE NDIFE Mkwatibwi Wake yemwe wawavomereza ndi kuwalandira Mawu Ake. Timafuula kuchokera pansi pamtima kuti:
Ndine Wanu, Ambuye. Ine ndikudzigoneka ndekha pa guwa ili, basi modzipatula monga ine ndikudziwira kuti ndidzipange ndekha. Tengani dziko lichoke mwa ine, Ambuye. Tengani zinthu kuchokera kwa ine zomwe ziri zakutha; ndipatseni ine zinthu zosatha, Mawu a Mulungu. Mundirole ine ndikhoze kumakhala moyo Mawu amenewo mwapafupi kwambiri, mpaka Mawu akhale ali mwa ine, ndi ine mu Mawu. Perekani izi Ambuye. Mundirole ine ndisadzachoke konse kwa Iwo.
Pali moyo, ndipo pali imfa. Pali njira yolondola, ndipo pali njira yolakwika. Pali choonadi, ndipo pali bodza. Uthenga uwu, Liwu ili, ndi njira yangwiro yoperekedwa ndi Mulungu ya lero. Bwerani mudzajowine gawo la Mkwatibwi wamphamvu wa Mulungu pamene tikusonkhana mozungulira Mawu Ake owululidwa ndi kumva Uthenga: Chitsutso 63-0707M.
M’bale. Joseph Branham
25-0914 Kodi Moyo Wanu Ndi Woyenera Uthenga?
Uthenga: 63-0630E Kodi Moyo Wanu Ndi Woyenera Uthenga?
- 25-0914 Kodi Moyo Wanu Ndi Woyenera Uthenga?
- 23-1008 Kodi Moyo Wanu Ndi Woyenera Uthenga?
- 22-0415 Kodi Moyo Wanu Ndi Woyenera Uthenga?
Okondedwa Abale ndi Alongo,
Ine ndimawakonda Ambuye, Mawu a Mulungu, Uthenga uwu, Liwu Lake, mneneri Wake, Mkwatibwi Wake, kuposa moyo iwomwini. Onse ali MMODZI KWA INE. Ine sindikufuna konse kunyengerera pa cholemba chimodzi, kachidutswa kamodzi, kapena MAWU AMODZI amene Mulungu anawalemba mu Mawu Ake kapena anayankhula kupyolera mwa mneneri Wake. Kwa ine, Zonse ndi Atero Yehova.
Mulungu ankaganiza Izo, ndiye anayankhula Izo kwa aneneri Ake, ndipo iwo analemba Mawu Ake. Ndiye Iye anatumiza mngelo Wake wamphamvu, William Marrion Branham, ku dziko lapansi mu tsiku lathu kotero kuti Iye akhoze kudziulula Yekha mu thupi la munthu kamodzinso, monga Iye anachitira ndi Abrahamu. Ndiye Iye analankhula kupyolera mwa mneneri Wake kuti akhale Liwu la Mulungu kwa dziko, kuti awulule ndi kutanthauzira zinsinsi zonse zimene zabisika kuchokera ku maziko a dziko kwa Mkwatibwi Wake wokonzedweratu.
Tsopano, Mkwatibwi Wake, INU, mukukhala Mawu osandulika thupi; Mmodzi ndi Iye, Mkwatibwi Wake wa Mawu wobwezeretsedwa kwathunthu.
Ndikudziwa kuti sindikumvetsetsa zomwe ndikunena komanso zomwe ndimalemba. Ndiloleni ndinene modzichepetsa monga momwe mneneri wathu ananenera, sindine wophunzira ndipo ndikudziwa kuti sindingathe kulemba kapena kulankhula molondola zimene ndikumva mumtima mwanga. Ndikuvomereza kuti zikuwoneka ngati ndimalemba mwawukali nthawi zina. Pamene nditero, sikusonyeza kupanda ulemu, kapena kukhala ndi maganizo olakwika kapena kuweruza wina, koma mosiyana. Ndimachita izi chifukwa chokonda Mawu a Mulungu mumtima mwanga.
Ine ndikufuna kuti aliyense avomereze ndi kukhulupirira Uthenga uwu umene Mulungu anatumiza kudzayitana Mkwatibwi Wake. Sindinamvepo mumtima mwanga kapena malingaliro anga kuti atumiki sayenera kulalikiranso; zikanakhala zikutsutsana ndi Mawu a Mulungu. Ndine wachangu chabe pa Mau a Mulungu pa matepi. Ine ndikukhulupirira kuti ndilo Liwu lofunika kwambiri lomwe ATUMIKI ONSE ayenera kuyika POYAMBA pamaso pa anthu. Izi sizikutanthauza kuti sangathe kulalikira, ndikungofuna kuwalimbikitsa kuti azisewera matepi mu mipingo yawo pamene anthu asonkhana pansi pa kudzoza kumeneko.
Inde, ndikanakonda kukhala ndi dziko lonse lapansi likumvetsera Uthenga womwewo nthawi imodzi padziko lonse lapansi. Osati chifukwa “ine” ndinanena chomwecho, kapena chifukwa “Ine” ndinasankha tepi kuti ndimvetsereko, koma ine ndikumverera ndithudi Mkwatibwi akanawona momwe Mulungu wakonzera njira kuti izi zichitike mu tsiku lathu.
Ngati ife tikanakhala nazo zojambulidwa za Yesu akuyankhula lero pa tepi, osati Mateyu, Marko, Luka kapena zolemba za Yohane za zomwe Yesu ananena (pakuti iwo onse ananena izo mosiyana pang’ono), koma nkumakhoza kumva Liwu la Yesu, umunthu Wake, makutu Ake, ndi makutu athu omwe, kodi utumiki lero unganene kwa mpingo wawo, “Ife sitidzasewera zojambulidwa za Yesu kuti ndizilalikira kwa Inu ndi kudzozedwa kwa izo mu mpingo wathu. Ine ndi woyitanidwa ndi odzozedwa kuwulalikira Iwo ndikumaubwereza iwo. Inu basi muzikavetsera ku Iwo mukapita kunyumba kwanu.” Kodi anthu angakhoze kumayima ndi zimenezo? N’zomvetsa chisoni kuziyankhula kuti zimenezi ndendende n’zimene akuchita lero lino. PALIBE KUSIYANA, ziribe kanthu momwe Iwo amachipanga icho kukhala choyera.
Kwa ine, M’bale Branham anatipatsa ife chitsanzo. Iye ankakonda pamene mipingo yonse, nyumba, kapena kulikonse kumene iwo anali, anali pa kulumikizana kotero kuti iwo azitha kumva Uthenga onse nthawi imodzi. Iye ankadziwa kuti iwo akanakhoza, ndipo akanati, awatenge matepi ndi kuwamva iwo kenako, koma iye ankawafuna iwo kuti akhale olumikizana ndi kumamva Uthenga onse pa nthawi imodzi…. KWA INE UMO NDIMOMWE ANALILI MULUNGU AKUSONYEZA MKWATIBWI WAKE MOMWE ZIDZAKHALIRE MU TSIKU LATHU NDI ZOYENERA KUCHITA.
Mtumiki woona aliyense wokhulupirira Uthenga adzavomereza kuti palibe chachikulu kuposa kukhala pansi pa kudzoza kwa Liwu la Mulungu, limene linajambulidwa ndi kuikidwa pa matepi. Mkwatibwi adzakhulupirira, ndi kukhala ndi Vumbulutso, kuti Uthenga uwu ndi Mawu a Mulungu a lero. Ine ndikhoza kungoweruza ndi Mawu, koma aliyense amene sakanati Uthenga uwu uli Mtheradi wawo alibe Vumbulutso la Mawu la lero, chotero, iwo angakhoze bwanji kukhala Mkwatibwi Wake?
Sikuti kumangobwereza izo, kulalikira kapena kuziphunzitsa izo, koma kuzimva izo pa matepi ndi MALO OKHAWO omwe Mkwatibwi anganene kuti ine ndimakhulupirira Mawu aliwonse. Uthenga uwu uli PAKUTI ATERO AMBUYE. Chimene ine ndimalalikira kapena kuphunzitsa si PAKUTI ATERO AMBUYE, koma chimene Liwu la Mulungu limanena pa matepi CHILI…
Ine ndikudziwa alipo abale ndi alongo amene amati, ndi kumverera, “Ngati inu simukumvera Uthenga wa Branham Tabernacle nsanamira, kuwerenga makalata a Mphungu Zikusonkhana, ndi kumamvetsera mnyumba zanu pa nthawi yomweyo inu simuli Mkwatibwi,” kapena, “Ndi kulakwa kupita ku tchalitchi, inu muyenera kukhala mnyumba mwanu.” NDIKULAKWA KWAMBIRI. Ine sindinayambe ndaganizapo zimenezo, kunena izo, kapena kukhulupirira izo. Izo zapangitsa ngakhale kupatukana kochuluka, zomverera zolimba, ndi kuchotsedwa pakati pa Mkwatibwi ndipo mdani akugwiritsa ntchito izo kuwalekanitsa anthu.
Ine sindikufuna konse kumulekanitsa Mkwatibwi, ine ndikufuna kuti ndimulumikize Mkwatibwi monga Mawu ananenera TIYENERA KUKHALA WOLUMIKIZANA NGATI MMODZI. Ife tisamakangane wina ndi mzake, koma palibenso china mophweka chimene chingatilumikizitse ife koma Liwu la Mulungu pa matepi.
Ife Sitiyenera kumakangana ndikuuza anthu zomwe AYENERA KUCHITA kapena kuti iwo si Mkwatibwi, inuyo ingochitani monga AMBUYE AKUKUTSOGOLERANI. Iwo akali abale ndi alongo athu. Tifunika kukondana ndi kulemekezana.
Tsopano, musakangane. Mwaona? Kupsa mtima kumabweretsa mkwiyo. Chinthu choyamba inu mukudziwa, inu mukukwiyitsa Mzimu Woyera kuchoka kwa inu, inu mudzakhala mukukangana mobwezera. Ndiye Mzimu Woyera umayamba kuwuluka. Kupsa mtima kumabweretsa mkwiyo.
Ndi zimene mneneri ananena apa, ine sindikufuna konse kumvetsa chisoni Mzimu Woyera. Sindikufuna kukangana. Titha kukambirana mwachikondi, koma osati kukangana. Ngati ndalankhula chilichonse chomwe chakhumudwitsa wina aliyense mu zomwe ndalemba kapena kunena, ndikhululukireni, sichinali cholinga changa.
Monga ndanenera kale, ndikumva kuitana pa moyo wanga kuchokera kwa Ambuye kuti ndilole anthu ku Mawu a Mulungu lero. Atumiki ena ali ndi maitanidwe ena ndipo mwina amawona zinthu mosiyana. Utumiki wanga ndi kungomuuza Mkwatibwi kuti, “KUKANIKIZA KUSEWERA” ndi “Liwu la Mulungu pa matepi ndilo Liwu lofunika kwambiri limene mungamve.” “Ine ndikukhulupirira kuti utumiki uyenera kumasewera Liwu la Mulungu pa matepi mu mipingo yawo.”
Makalata amene ine ndimalemba sabata iliyonse ndi a gawo la Mkwatibwi amene amadzimva kuti ali gawo la Branham Tabernacle. Ndikudziwa kuti ena ambiri amawawerenga, koma ndili ndi udindo wochita zomwe ndikumverera kuchitidwa mu tchalitchi chathu. Mpingo uliwonse uli wa pawokha; iwo ayenera kuchita monga iwo akumverera kutsogozedwa ndi Ambuye kuti achite, ndiwo 100% Mawu. Ine Sindikutsutsana nawo iwo, timangosagwirizana. Kwa ine ndi Branham Tabernacle, ife tikungofuna kokha basi kuti tizimva Liwu la Mulungu pa matepi.
Ine Ndimaitana dziko kuti lizijowinana nafe sabata iliyonse. Ndimawalimbikitsa kuti ngati sangathe kujowinana nafe, kusankha tepi, tepi iliyonse, ndikuyikanikiza kuisewera iyo. Iwo adzadzozedwa kuposa kale. Kotero, ine ndikukuitanani inu sabata ino kuti mudzajowinane nafe Lamlungu pa 12:00 P.M., nthawi ya ku Jeffersonville, pamene ife tidzasonkhana pamodzi ndi kumva, 63-0630E Kodi Moyo Wanu Ndi Woyenera Uthenga?
M’bale Joseph Branham
25-0907 Kutuluka Kwachitatu
Uthenga: 63-0630M Kutuluka Kwachitatu
25-0831 Ukulirira Chiyani? Yankhula!
Uthenga: 63-0714M Ukulirira Chiyani? Yankhula!
- 25-0831 Ukulirira Chiyani? Yankhula!
- 23-1022 Ukulirira Chiyani? Yankhula!
- 22-0417 Ukulirira Chiyani? Yankhula!
- 20-0426 Ukulirira Chiyani? Yankhula!
- 19-0804 Ukulirira Chiyani? Yankhula!
- 17-0604 Ukulirira Chiyani? Yankhula!
Wokondedwa Mpingo wa Mulungu,
Mulungu analankhula nati, ““Ine sindigwira ntchito pa dziko lapansi, kupatula kupyolera mwa munthu. Ine—Ine—Ine ndine Mpesa; inu ndinu nthambi. Ndipo ine ndimadzifotokoza kokha Inemwini pamene ine ndingakhoze kupeza munthu M’MODZI. Ndipo Ine ndamusankha iye, William Marrion Branham. Ine ndamutumiza iye kumusi kuti adzaitane Mkwatibwi Wanga. Ine ndidzaika Mau anga mu mkamwa mwake . Mau anga adzakhala Mau ake. Iye adzalankhula Mau anga ndi kumalankhula zokhazo zomwe ine ndimalankhula.
Liwu la Lemba linayankhula kupyolera mu Lawi la Moto ndipo linamuuza iye, “Ine ndakusankha iwe, William Branham. Iwe ndi mwamunayo. Ine ndinakulera iwe kwa cholinga ichi. Ine ndidzakutsimikizira iwe mwa zizindikiro ndi zodabwitsa. Iwe ukupita ku dziko la pansi kuti ukaulule Mawu Anga ndi kukamutsogolera Mkwatibwi Wanga. Mawu Anga ayenera kuti akwaniritsidwe ndi IWE.”
Mneneri wathu ankadziwa kuti anatumidwa ndi cholinga chomwecho kuti aulule zinsinsi zonse za Baibulo ndi kutsogolera Mkwatibwi wa Mulungu ku Dziko Lolonjezedwa. Iye ankadziwa chimene iye ananena, Mulungu akanadzalemekeza ndi kuchikwaniritsa. Ine ndikufuna kuti inu musamaiwale Mawu amenewo. Zimene mneneri wathu ananena, Mulungu azilemekeza, chifukwa Mawu a Mulungu anali mwa William Marrion Branham. Iye ali Liwu la Mulungu kwa dziko.
Iye ankadziwa kuti iye anali mngelo wodzozedwa wa Mulungu. Iye ankadziwa mumtima mwake zonse zimene Mulungu ananena zokhudza iye m’Mawu ake. Zomwe zinkamudetsa nkhawa kwambiri zinali zitachitikadi. Iye anali wodzozedwa ndipo ankadziwa kuti iye anali ndi PAKUTI ATERO AMBUYE. Palibe chimene chikanamuletsa kupita kukalankhula Mawu a Mulungu.
Mulungu anamuuza iye, “Mawu Anga, ndi iweyo, Mtumiki Wanga, muli ofanana.” Iye ankadziwa kuti iye ndi amene anasankhidwa kulankhula Mawu osalephera. Ndizo zonse zomwe iye adafunitsitsa. Iye AMATHA KUYANKHUL A, NDIPO MULUNGU ANKACHITITSA ICHO KUKWANILITSIDWA.
Vumbulutso la Uthenga uwu NDI mthenga wa Mulungu wadzoza chikhulupiriro chathu KUPOSA momwe zisanachitikepo mkale lonse. Izo zatisunthira ife mu magulu aakulu kwambiri. Izo zatilekanitsa ife ku chirichonse kupatula Uthenga Wake, Mawu Ake, Liwu Lake, Matepi Ake.
Ziribe kanthu kuti ndife ochepa bwanji, timasekedwa mochuluka bwanji, kunyozedwa, sizimatitekesa mpang’ono pomwe. IFE TIMACHIONA ICHO. IFE TIMAKHULUPIRIRA ICHO. Pali chinachake mkati mwathu. Tinakonzedweratu kuti tidzachiwone ICHO ndipo palibe chimene chidzaatilepheretsa ife kuchikhulupirira ICHO.
Ife timakumbukira zomwe masomphenyawo ananena, “bwerera ukasunge Chakudya”. Kodi nkhokweyo inali kuti? Branham Tabernacle. Kodi pali chirichonse mu dziko, kapena kuzungulira dziko kulikonse, chimene chingafanane ndi Mauthenga amene ife tiri nawo? IWO ndi Liwu lokhalo lotsimikiziridwa ndi Mulungu Mwiniwake kuti liri PAKUTI ATERO AMBUYE. LIWU LOKHALO!
Kodi ndi kutiso kumene ife tikanati, kapena tikanafuna kupita, pamene iye anati;
Apa ndi pomwe Chakudyachi chasungidwira…
Icho chasungidwa pano
Iwo uli pa matepi. Iwo uzipita ku kutambalala konse kwa dziko pa matepi, kumene anthu mu manyumba mwawo. Matepi amenewo azikafika mmanja mwa a okonzedweratu a Mulungu. Iye akhoza kuwalondolera Mawu. Iye alondolera chirichonse ndendende basi mpaka ku ntchito yake. Ndicho chifukwa Iye ananditumiza Ine kuti ndibwerere ndidzachite izi. “Kudzachisunga Chakudyacho kuno.”
Ife Ndife Mkwatibwi wa Mawu Ake Angwiro amene wakhala ndi Chakudya Chake Chosungidwa. Palibe chifukwa chomaliranso, ife timangoyankhula Mawu ndi kupita patsogolo, pakuti ife NDIFE Mawu.
Palibe chomadela nkhawa. Palibeso chifukwa chomakhalira ndi misonkhano ya mapemphero ausiku onse kuti itiwululire kuti ife ndife ndani, Mawu avumbulutsidwa kwa ife. Timadziwa kuti ndife ndani, mofanana ndi mneneri wa Mulungu, ndipo watiuza kale amene anali kupita.
“Mmodzi aliyense wa ife! Kaya ndinu mkazi wa mnyumba, kapena ndinu m—mdzakazi wamng’ono, kapena ndinu mkazi wachikulire, kapena mwamuna wamng’ono, kapena mwamuna wachikulire, kapena chirichonse chimene inu muli, ife tikupita, mulimonse. Sipakhala mmodzi wa ife ati atsalire.” Ameni. “Mmodzi aliyense wa ife akupita, ndipo ife sitiletsa kanthu kalikonse.”
Lankhulani za kutipatsa ife CHIKHULUPILIRO chokwatulitsa!!!
Bwerani mudzajowine gawo la Mkwatibwi wa Mulungu pamene ife tikusonkhana palimodzi mozungulira Liwu lotsimikiziridwa la Mulungu, pamene Iye akuyankhula ndi kutiuza ife: Wokondedwa Wanga, Wosankhidwa Wanga, Mkwatibwi Wanga, Ukulilira Chiyani, Yankhula, ndipo pita patsogolo.
M’bale. Joseph Branham
Uthenga: 63-0714M Ukulilira Chiyani? Yankhula!
Nthawi: 12:00 PM, Nthawi yaku Jeffersonville
Malo:
Koma pali Mpingo weniweni umodzi wokha, ndipo iwe sumajowina Iwo. Iwe umabadwira mwa Iwo. Mwaona? Ndipo ngati iwe wabadwira mwa iwo, Mulungu wamoyo amagwira ntchito Iyemwini kupyolera iwe, ndi kumadzipangitsa Iyemwini kudziwika. Mwaona? Ndiko kumene Mulungu amakhala, mu Mpingo Wake. Mulungu amapita ku Tchalitchi tsiku lirilonse, amakhala moyo mu Mpingo. Iye amakhala moyo mwa inu. Inu ndinu Mpingo Wake. Inu ndinu Mpingo Wake. Inu ndinu Kachisi amene Mulungu amakhalamo. Ndinu Mpingo wa Mulungu wamoyo, inueni.
25-0824 Mgonero
Uthenga: 65-1212 Mgonero
Wokondedwa Mawu Otsimikiziridwa Mkwatibwi Yekha,
Ndife othokoza bwanji kwa Mzimu Woyera chifukwa cha Vumbulutso loona la Mawu Ake otsimikiziridwa a lero. Ambiri amadzinenera kuti amakhulupirira M’bale Branham kuti ndi mneneri wa Mulungu amene amakwaniritsa Malemba olonjezedwa a iyemwini, koma Vumbulutso loona la Mawu ndi dongosolo la Mulungu labisika kwa iwo.
Ndi kalata yachikondi iliyonse yomwe Mkwatibwi amamva, Mulungu amatsimikizira kwa ife kuti tili mu Chifuniro Chake changwiro pomvera Njira Yake yoperekedwa ya lero, Liwu la Mulungu pa Matepi.
Ndipo ife tikuyenera kumutsatira Iye, ndiyo njira yokhayo yokhalira nawo Moyo Wamuyaya. Chotero utsogoleri wa Mulungu ndi: kutsatira Mawu otsimikiziridwa a ora mwa Mzimu Woyera.
NJIRA YOKHA yopita ku Moyo Wamuyaya ndi: Mzimu Woyera ukukutsogolerani kuti muzitsatira Mawu otsimikiziridwa. Ndani ali nawo Mawu otsimikiziridwa a lero? Kodi Mulungu anamusankha ndani kuti azitanthauzira Mawu Ake? Kodi Mulungu ananena kuti linali liwu lake la ndani lero? Kodi Mulungu Mwiniwake anati ndani anali mtsogoleri wotsimikiziridwa kuti atsogolere Mkwatibwi Wake lero? Utumiki?
Chimodzimodzi monga ine ndinanena, mphungu yaing’ono pamene iyo inamva Liwu la Mkwati, iyo inapita kwa ilo, odzozedwa, Mawu otsimikiziridwa a Mulungu a tsiku lotsirizali.
Nowa anali Mawu otsimikiziridwa a tsiku lake.
Mose anali Mawu otsimikiziridwa a tsiku lake.
Yohane anali Mawu otsimikiziridwa
Iwo akhoza kupotoza chirichonse kapena kutanthauzira kulikonse kwa Iwo akufuna, koma:
WILLIAM MARRION BRANHAM NDI MAWU OTSIMIKIZIRIDWA A MULUNGU A LERO!!
Chotero utsogoleri wa Mulungu ndi: kutsatira Mawu otsimikiziridwa a ora mwa Mzimu Woyera.
Ndipo kusewera Liwu lotsimikiziridwa la Mulungu mu mpingo wanu si chinthu chofunika kwambiri chimene Mkwatibwi angachite? Ndikofunikira kwambiri kumva liwu losiyana?
Kodi ndi gulu la amuna ndi utumiki wawo umene udzalumikizana ndi kutsogolera Mkwatibwi? Kodi Mkwatibwi adzalumikizidwa ndi zomwe utumiki ukunena? Onse akunena zosiyana, ndiye titsatire ndani?
Kodi kutanthauzira kwawo kwa Uthenga uwu ndi kumene ife tidzaweruzidwa nako? Kodi iwo ali nalo Lawi la Moto likutsimikizira utumiki wawo? Kodi ndiko kutanthauzira kwawo kwa Mawu Mtheradi wanu?
Mneneri anati Mkwatibwi adzakhala WOLUMIKIZANA. Dzifunseni nokha, ndi chiyani chiti chidzachititse uneneri uwu kuti ukwanilitsidwe kuti Ambuye abwere ndi kudzamukwatula Mkwatibwi Wake?
Ndiyeno, pamene anthu a Mulungu ayamba kusonkhananso palimodzi, pamakhala chiyanjano, pamakhala mphamvu. Mukuona? Ndipo paliponse pamene anthu a Mulungu abwera palimodzi kwathunthu, ine ndikukhulupirira chiukitsiro chidzachitika apo ndiye. Padzakhala nthawi ya mkwatulo pamene Mzimu Woyera udzayamba kuwasonkhanitsa iwo. I—iwo adzakhala apang’ono, ndithudi, koma kudzakhala kuli kusonkhana kwakukulu.
Kodi padzakhala kusonkhana kwakukulu kuzungulira utumiki wa munthu wina, kupatulapo mneneri wotsimikiziridwa wa Mulungu? Kodi lidzakhala GULU la atumiki chifukwa ena mwa awutumiki wofutukuka pasanu amanena kuti MUSAMASEWERE LIWU la Mulungu mu tchalitchi mwanu, ndi zolakwika. Kodi iwo adzatsogolera Mkwatibwi ndiye?
CHONDE NDITHANDIZENI! KODI NDI MTUMIKI UTI YEMWE NDIYENERA KUMUTSATIRA POMWE NDIKUFUNA KUKHALA WOLUMIKIDWA NAWO PA PAMSONKHANO WAWUKULU UWO.
Ena amati utumiki wofutukuka pasanu a Mabingu Asanu ndi awiri adzafikitsa Mkwatibwi ku ungwiro . Atumiki ena awutumiki wofutukuka pasanu amati masiku a utumiki wa Munthu Mmodzi atha. Atumiki ena a utumiki wofutukuka pasanu amati ife tiyenera kubwerera ku Pentekosite. Ena amati Uthenga SULI M’theradi. Ena amati ukamasewera matepi ndiwe wokhulupirira milungu. Onse amanena chinachake chosiyana, ndipo ONSE ali ndi matanthauziridwe osiyana, malingaliro osiyana, koma aliyese wa iwo amanena kuti IWO akutsogozedwa ndi Mzimu Woyera.
KODI NDI MTUMIKI WUTI WA UTUMIKI WOFUTUKUKA PASANU YEMWE NDIYENERA KUMUTSATIRA? Bola ngati ine nditsatila abusa “ANGA” awutumiki wofutukuka pasanu, ine ndidzakhala Mkwatibwi? Pali “Magulu” osiyanasiyana a atumiki wofutukuka pasanu. Atumiki 20 awa amasonkhana pamodzi ndi kuchititsa misonkhano yawo, koma 20 amatsutsana kwathunthu ndi azitumiki ena amene akukhala ndi misonkhano yosiyana…ndi misonkhano iti yomwe ine ndipite kuti ndikakhale wangwiro ndi wolumikizana…ena a iwo…onse a iwo?
Ndipo anthu amakhulupilira kuti CHISOKONEZO CHIMENECHI CHILUMIKIZITSA NDIKUMUFIKITSA KU UNGWIRO MKWATIBWI? Onse amati iwo ali Atumiki WOONA AWUTUMIKI WOFUTUKUKA PASANU WOITANIDWA NDI MULUNGU. Koma iwo sakukutsogolerani inu ku UTSOGOLERI WOONA WA MZIMU WOYERA, AKUKUKUTSOGOLERANI INU KWA IWO ENI NDIKU UTUMIKI WAWO.
Kwa ine, simukusowa ngakhale vumbulutso kuti mudziwe zomwe sizingagwirizane kapena kutsogolera Mkwatibwi yense. MAWU OKHA ati adzayanjanitse Mkwatibwi, mwa LIWU LA MULUNGU YEKHA PA MATEPI.
Abale ndi alongo, kulibwino kuti mudzuke ngati mukutsatira m’busa amene akungolalikira ndi kubwereza mawu Mawu, omwe ali odabwitsa ndipo ALI NDENDENDE chimene ayenera kuchita, koma osakuuzani, ndipo chofunika kwambiri, KUCHITA, posewera LIWU LA MULUNGU PA MATEPI MU MPINGO WANU.
M’bale Branham anatiuza kuti:
Tsopano, ife tiri ndi madongosolo Auzimu atatu okha omwe atsalira kwa ife: amodzi a iwo ndi—ndi mgonero, kutsukana-mapazi, ubatizo wa madzi. Ndi zinthu zitatu zokhazo. Ndiwo ungwiro, wa zitatuzo, mwaona.
Ine ndikufuna kuti ife tikhale ndi Chiyanjano cha Mgonero ndi kutsukana Mapazi Lamlungu lino, ngati Ambuye alola. Monga tinachitirapo m’mbuyomu, ndikukulimbikitsani inu kuti muyambe nthawi ya 5:00 PM. Mu nthawi ya m’dera lanu . Ngakhale kuti M’bale Branham ananena kuti atumwi amadya Mgonero nthawi iliyonse imene iwo ankasonkhana, iye ankakonda kuti azidya iwo nthawi yamadzulo, ndipo ankawutchula kuti Mgonero wa Ambuye.
Utumiki wa Uthenga ndi Mgonero udzakhala pa Wailesi ya Liwu, ndipo padzakhalanso ulalo wa fayilo yomwe mungatsitse, kwa iwo omwe sangathe kupeza Wilesi ya Liwu Lamlungu madzulo.
M’bale Joseph Branham
25-0817 Utsogoleri
Uthenga: 65-1207 Utsogoleri
Wokondedwa Mkwatibwi wa Khristu, tiyeni tibwere palimodzi Lamlungu nthawi ya 12:00 P.M., nthawi yaku Jeffersonville, kuti tidzamve 65-1207 Utsogoleri.
Mbale. Joseph Branham