Uthenga: 64-0617 Khristu Wozindikiritsidwa Wa Mibadwo Yonse
- 25-1116 Khristu Wozindikiritsidwa Wa Mibadwo Yonse
- 20-0809 Khristu Wozindikiritsidwa Wa Mibadwo Yonse
- 17-0208 Khristu Wozindikiritsidwa Wa Mibadwo Yonse
Wokondedwa Mawu Amoyo a Mulungu,
Zaka zonsezi ine ndakhala ndikuzibisa izo mu mtima mwanga, kumuphimba Khristu, Lawi la Moto lomwe lija likutanthauzira Mawu, monga zinalonjezedwa.
Ndikudziwa kuti izi zimveka mopanda nzeru kwa anthu ambiri, koma ngati mungopirira ndi mthenga wa mngelo wa Mulungu kwa mphindi zochepa, ndikupempha Mulungu kuti akupatseni vumbulutso lowonjezera, ndikukhulupirira kuti iye, mothandizidwa ndi Mulungu komanso ndi Mawu Ake, komanso molingana ndi Mawu Ake, adzamubweretsa Iye pano pamaso panu. Mulungu, akuulula ndi kudziwonetsera Yekha, kutanthauzira ndi kuulula Mawu Ake.
Ndi chitsitsimutso chotani chomwe chakhala chikuchitika mwezi watha uno mkati mwa Mkwatibwi wa Yesu Khristu. Mulungu, akuulula Yekha kuposa kale lonse, akulankhula ndi Wokondedwa Wake, kupanga chikondi ndi Iye, kumutsimikizira, Ndife Amodzi ndi Iye.
Palibe kukayikira, palibe kusatsimikizika, palibe kukayikira, ngakhale mthunzi wa kukayikira; Mulungu watiululila kwa ife: Liwu la Mulungu likulankhula pa matepi ndi NJIRA YOPEREKEDWA NDIPOSO NJIRA YANGWIRO KWA MKWATIBWI WAKE LERO.
Anapereka njira iyi kuti tisadzafunikire iyo kuisefa, kuifotokoza, kapena kuigwiritsa ntchito mwa umunthu mwanjira iliyonse; zingomverani kokha basi Liwu Loyera la Mulungu likulankhula kuchokera ku mulomo kupita ku khutu kwa aliyense wa ife.
Iye adadziwa kuti tsiku lino likubwera. Iye adadziwa kuti Mkwatibwi Wake angadzadye Manna Obisika okha, Chakudya Chake cha Nkhosa. Sitikufuna kumva china chilichonse kupatula Mawu a Mulungu ochokera kwa Mulungu Mwiniwake.
Ife tadutsa chophimba chimenecho kulowa mu Ulemerero wa Shekinah. Dziko lapansi silingathe kuwona. Mneneri wathu sangatchule mawu ake moyenera. Sangavale bwino. Sangavale zovala za ubusa. Koma kuseri kwa chikopa cha munthu, mkati mwake muli Ulemerero wa Shekinah. Mkati mwake muli mphamvu. Mkati mwake muli Mawu. Mkati mwake muli Mkate Wowonetsera. Mkati mwake muli Ulemerero wa Shekinah, womwe ndi Kuwala komwe kumakhwimitsa Mkwatibwi.
Ndipo kufikira inu mutabwera kuseri kwa chikopa cha katumbu chimenecho, kufikira inu mutatuluka mu chikopa chanu chakale, maganizo anu akale, tizikhulupiriro tanu takale, ndi kubwera mu Kukhalapo kwa Mulungu; pamenepo Mawu amadzakhala chenicheni chamoyo kwa inu, pamenepo inu mumadzutsidwira ku Ulemelero wa Shekinah, zikatero Baibulo limadzakhala Bukhu latsopano, pamenepo Yesu Khristu amakhala yemweyo dzulo, lero, ndi kwanthawizonse. Inu mukukhala mu Kukhalapo Kwake, mukudya mkate wopanda chotupitsa umene wangoperekedwa tsiku limenelo kwa okhulupirira, ansembe okha. “Ndipo ife tiri ansembe, unsembe wachifumu, fuko loyera, anthu achilendo, akupereka nsembe zauzimu kwa Mulungu.” Koma inu mukuyenera kulowa mkati, kuseri kwa chophimba, kuti mukamuwone Mulungu wovundukulidwa. Ndipo Mulungu wavundukulidwa, ndiwo Mawu Ake akuwonetseredwa.
Ndife anthu osamvetseka ku dziko lapansi, koma ife ndi ukhutitsidwa kudziwa kuti Bauti wathu ndi ndani ndiposo onyadira kukhala nati ya matepi Ake, olumikizidwa ku Mawu Ake, chifukwa amatikokera kwa Iye.
Ngati simulumikizidwa ku matepi, siyinu chinthu china koma mulu wa chiphakasa!!!
Tsopano, zindikirani tsopano, Mulungu! Yesu ananena kuti, “Iwo amene Mawu amabwerako, ankatchedwa ‘milungu,’” amenewo anali aneneri. Tsopano, osati munthuyo iyemwini anali Mulungu, osatinso kuti thupi la Yesu Khristu linali Mulungu. Iye anali munthu, ndipo Mulungu amaphimbidwa kuseri kwa Iye.
Mulungu, tsiku lina adaphimbidwa kuseri kwa chikopa cha katumbu. Mulungu, tsiku lina ataphimbidwa ndi thupi la munthu wotchedwa Melkizedeki. Mulungu, adaphimbidwa ndi thupi la munthu wotchedwa Yesu. Mulungu, adaphimbidwa ndi thupi la munthu wotchedwa William Marrion Branham. Mulungu, adaphimbidwa ndi thupi la munthu wotchedwa MKWATIBWI WAKE.
Izo kotero ndikofunikira kukumbukira, koma ambiri akulephera ndipo iwo akuyang’ana china chake basi. Chinthu chomaliza chimene Abrahamu anaona, chinthu chomaliza kuchitika moto usanagwe ndi kuweruza dziko la Amitundu, mwana wolonjezedwa asanabwere, chinthu chomaliza chimene mpingo wachikhristu udzawona mpaka kuwonekera kwa Yesu Khristu ndi Melkizedeki, Mulungu woonekera mu m’thupi, akuulula Mawu Ake kwa Mkwatibwi Wake.
Palibe china chilichonse chomwe chikubwera. Palibe china chilichonse chomwe chinalonjezedwa m’Mawu Ake. Palibe munthu, kapena gulu la anthu lomwe lidzabwere kudzamupanga wangwiro Mkwatibwi.
Ayi! Iwo akufuna kuti azibwera kuno ku mpingo kuti akhale angwiro. Mukuona? Kuti i—ife timapeza chiyanjano wina ndi mzake kuno ku mpingo, koma ungwiro umabwera mwa pakati pa ife ndi Mulungu. Magazi a Khristu ndi amene amatipanga ife angwiro mwa Mzimu Woyera.
Uthenga uwu, Liwu ili, Mawu otsimikiziridwa a Mulungu, akumupanga kukhala wangwiro Mkwatibwi wa Yesu Khristu.
Ndikukupemphani aliyense wa inu kuti abwere kudzamvetsera nafe Liwu la Mulungu pamene likumupanga kukhala wangwiro Mkwatibwi Wake Lamlungu lino nthawi ya 12:00 PM, nthawi ya ku Jeffersonville, pamene tikumva: 64-0617 “Khristu Wozindikiritsidwa Wa Mibadwo Yonse”.
M’bale Joseph Branham
Malemba oti muwerenge Uthenga usanaperekedwe:
Deuteronomo 18:15
Zakariya 14:6
Malaki 3: 1-6
Luka Woyera 17: 28-30
Yohane Woyera 1: 1 / 4: 1-30 / 8: 57-58 / 10: 32-39
Ahebri 1: 1 / 4: 12 / 13: 8
Chivumbulutso 22: 19