Category Archives: Uncategorized

25-0921 Chitsutso

Uthenga: 63-0707M Chitsutso

PDF

BranhamTabernacle.org

Okondedwa Iwo Omasulidwa,

Tsopano, kumeneko, “iwo,” osati wochimwa. “Iwo,” amenewo ndi, mpingo wa tsiku limenelo, iwo anapeza cholakwika ndi Munthu Yemwe anali Mawu. Ndi kulondola uko? Iwo anapeza cholakwika ndi Munthu Yemwe anali Mawu. Tsopano iwo akupeza cholakwika ndi Mawu akugwira ntchito kupyolera mwa munthu.

Kuyambira pachiyambi dziko lamukana Iye, linamukana Iye, linakana kukhala ndi Mawu Ake pa kusunga ndi miyambo yawo, zikhulupiriro zawo, malingaliro awo. Iwo nthawizonse amaphonya dongosolo la Mulungu; Mulungu, monga Munthu, yemwe anali Mawu, ndipo tsopano Mawu akugwira ntchito kupyolera mwa munthu.

Koma mu tsiku lathu Iye anati, “Ine ndidzakhala nawo gulu laling’ono, osankhidwa apang’ono, iwo anali mwa Ine kuchokera pachiyambi. Iwo adzandilandila Ine ndi kudzakhulupilira mau anga ndi Munthu yemwe Ine ndinamusankha kudzaulula mau anga. Iye adzakhala Liwu Langa kwa iwo

“Iwo sadzachita manyazi kulalikira Liwu Langa.” Iwo sadzachita manyazi kuuza dziko kuti Ine ndabwera kachiwiri ndipo ndadziwonetsera Ndekha kupyolera mu thupi la munthu monga Ine ndinanenera kuti Ine ndidzachita. Nthawi imeneyi iwo sadzamupembedza munthuyo, koma iwo azidzandipembedza Ine, Mawu, amene ati adzayankhule kupyolera mwa munthu. Adzandikonda Ine ndi kundilengeza mu m’tsempha uliwonse wa umunthu wawo.”

“Potero, Ine ndawapatsa iwo zonse zomwe iwo akusowa kuti akhale Mkwatibwi Wanga. Ine ndawalimbitsa iwo ndi Mawu Anga; pakuti iwo ALI MAWU ANGA atasandulika thupi. Ngati iwo akusowa machiritso, iwo alankhule Mawu Anga. Ngati iwo ali ndi chotchinga chirichonse chimene chimawatchinga iwo, iwo alankhule Mawu Anga. Ngati iwo ali ndi mwana yemwe walowelela, iwo alankhule Mawu Anga. Chirichonse chimene iwo akusowa, iwo alankhule Mawu Anga, pakuti iwo ali Mawu Anga opangidwa thupi mwa iwo.”

“Iwo akudziwa omwe iwo ali, pakuti Ine ndadziululira Inemwini kwa iwo. Iwo akhala owona ndi okhulupirika ku Mawu Anga ndipo akulumikizana palimodzi kuzungulira Liwu Langa.Pakuti iwo akudziwa Liwu Langa, Mawu Anga, Mzimu Wanga Woyera. Iwo akudziwa, kumene kuli Mawu, Mphungu zidzasonkhanitsidwa.”

Pamene mneneri Wake akulankhula Mawu Ake ndi kuwutsutsa m’badwo uno wa kumupachika Yesu Khristu kachiwiri ndi kulengeza kuti iwo awonongedwa, Mkwatibwi adzakhala akusangalala. Pakuti ife tikudziwa IFE NDIFE Mkwatibwi Wake yemwe wawavomereza ndi kuwalandira Mawu Ake. Timafuula kuchokera pansi pamtima kuti:

Ndine Wanu, Ambuye. Ine ndikudzigoneka ndekha pa guwa ili, basi modzipatula monga ine ndikudziwira kuti ndidzipange ndekha. Tengani dziko lichoke mwa ine, Ambuye. Tengani zinthu kuchokera kwa ine zomwe ziri zakutha; ndipatseni ine zinthu zosatha, Mawu a Mulungu. Mundirole ine ndikhoze kumakhala moyo Mawu amenewo mwapafupi kwambiri, mpaka Mawu akhale ali mwa ine, ndi ine mu Mawu. Perekani izi Ambuye. Mundirole ine ndisadzachoke konse kwa Iwo.

Pali moyo, ndipo pali imfa. Pali njira yolondola, ndipo pali njira yolakwika. Pali choonadi, ndipo pali bodza. Uthenga uwu, Liwu ili, ndi njira yangwiro yoperekedwa ndi Mulungu ya lero. Bwerani mudzajowine gawo la Mkwatibwi wamphamvu wa Mulungu pamene tikusonkhana mozungulira Mawu Ake owululidwa ndi kumva Uthenga: Chitsutso 63-0707M.

M’bale. Joseph Branham

25-0914 Kodi Moyo Wanu Ndi Woyenera Uthenga?

Uthenga: 63-0630E Kodi Moyo Wanu Ndi Woyenera Uthenga?

PDF

BranhamTabernacle.org

Okondedwa Abale ndi Alongo,

Ine ndimawakonda Ambuye, Mawu a Mulungu, Uthenga uwu, Liwu Lake, mneneri Wake, Mkwatibwi Wake, kuposa moyo iwomwini. Onse ali MMODZI KWA INE. Ine sindikufuna konse kunyengerera pa cholemba chimodzi, kachidutswa kamodzi, kapena MAWU AMODZI amene Mulungu anawalemba mu Mawu Ake kapena anayankhula kupyolera mwa mneneri Wake. Kwa ine, Zonse ndi Atero Yehova.

Mulungu ankaganiza Izo, ndiye anayankhula Izo kwa aneneri Ake, ndipo iwo analemba Mawu Ake. Ndiye Iye anatumiza mngelo Wake wamphamvu, William Marrion Branham, ku dziko lapansi mu tsiku lathu kotero kuti Iye akhoze kudziulula Yekha mu thupi la munthu kamodzinso, monga Iye anachitira ndi Abrahamu. Ndiye Iye analankhula kupyolera mwa mneneri Wake kuti akhale Liwu la Mulungu kwa dziko, kuti awulule ndi kutanthauzira zinsinsi zonse zimene zabisika kuchokera ku maziko a dziko kwa Mkwatibwi Wake wokonzedweratu.

Tsopano, Mkwatibwi Wake, INU, mukukhala Mawu osandulika thupi; Mmodzi ndi Iye, Mkwatibwi Wake wa Mawu wobwezeretsedwa kwathunthu.

Ndikudziwa kuti sindikumvetsetsa zomwe ndikunena komanso zomwe ndimalemba. Ndiloleni ndinene modzichepetsa monga momwe mneneri wathu ananenera, sindine wophunzira ndipo ndikudziwa kuti sindingathe kulemba kapena kulankhula molondola zimene ndikumva mumtima mwanga. Ndikuvomereza kuti zikuwoneka ngati ndimalemba mwawukali nthawi zina. Pamene nditero, sikusonyeza kupanda ulemu, kapena kukhala ndi maganizo olakwika kapena kuweruza wina, koma mosiyana. Ndimachita izi chifukwa chokonda Mawu a Mulungu mumtima mwanga.

Ine ndikufuna kuti aliyense avomereze ndi kukhulupirira Uthenga uwu umene Mulungu anatumiza kudzayitana Mkwatibwi Wake. Sindinamvepo mumtima mwanga kapena malingaliro anga kuti atumiki sayenera kulalikiranso; zikanakhala zikutsutsana ndi Mawu a Mulungu. Ndine wachangu chabe pa Mau a Mulungu pa matepi. Ine ndikukhulupirira kuti ndilo Liwu lofunika kwambiri lomwe ATUMIKI ONSE ayenera kuyika POYAMBA pamaso pa anthu. Izi sizikutanthauza kuti sangathe kulalikira, ndikungofuna kuwalimbikitsa kuti azisewera matepi mu mipingo yawo pamene anthu asonkhana pansi pa kudzoza kumeneko.

Inde, ndikanakonda kukhala ndi dziko lonse lapansi likumvetsera Uthenga womwewo nthawi imodzi padziko lonse lapansi. Osati chifukwa “ine” ndinanena chomwecho, kapena chifukwa “Ine” ndinasankha tepi kuti ndimvetsereko, koma ine ndikumverera ndithudi Mkwatibwi akanawona momwe Mulungu wakonzera njira kuti izi zichitike mu tsiku lathu.

Ngati ife tikanakhala nazo zojambulidwa za Yesu akuyankhula lero pa tepi, osati Mateyu, Marko, Luka kapena zolemba za Yohane za zomwe Yesu ananena (pakuti iwo onse ananena izo mosiyana pang’ono), koma nkumakhoza kumva Liwu la Yesu, umunthu Wake, makutu Ake, ndi makutu athu omwe, kodi utumiki lero unganene kwa mpingo wawo, “Ife sitidzasewera zojambulidwa za Yesu kuti ndizilalikira kwa Inu ndi kudzozedwa kwa izo mu mpingo wathu. Ine ndi woyitanidwa ndi odzozedwa kuwulalikira Iwo ndikumaubwereza iwo. Inu basi muzikavetsera ku Iwo mukapita kunyumba kwanu.” Kodi anthu angakhoze kumayima ndi zimenezo? N’zomvetsa chisoni kuziyankhula kuti zimenezi ndendende n’zimene akuchita lero lino. PALIBE KUSIYANA, ziribe kanthu momwe Iwo amachipanga icho kukhala choyera.

Kwa ine, M’bale Branham anatipatsa ife chitsanzo. Iye ankakonda pamene mipingo yonse, nyumba, kapena kulikonse kumene iwo anali, anali pa kulumikizana kotero kuti iwo azitha kumva Uthenga onse nthawi imodzi. Iye ankadziwa kuti iwo akanakhoza, ndipo akanati, awatenge matepi ndi kuwamva iwo kenako, koma iye ankawafuna iwo kuti akhale olumikizana ndi kumamva Uthenga onse pa nthawi imodzi…. KWA INE UMO NDIMOMWE ANALILI MULUNGU AKUSONYEZA MKWATIBWI WAKE MOMWE ZIDZAKHALIRE MU TSIKU LATHU NDI ZOYENERA KUCHITA.

Mtumiki woona aliyense wokhulupirira Uthenga adzavomereza kuti palibe chachikulu kuposa kukhala pansi pa kudzoza kwa Liwu la Mulungu, limene linajambulidwa ndi kuikidwa pa matepi. Mkwatibwi adzakhulupirira, ndi kukhala ndi Vumbulutso, kuti Uthenga uwu ndi Mawu a Mulungu a lero. Ine ndikhoza kungoweruza ndi Mawu, koma aliyense amene sakanati Uthenga uwu uli Mtheradi wawo alibe Vumbulutso la Mawu la lero, chotero, iwo angakhoze bwanji kukhala Mkwatibwi Wake?

Sikuti kumangobwereza izo, kulalikira kapena kuziphunzitsa izo, koma kuzimva izo pa matepi ndi MALO OKHAWO omwe Mkwatibwi anganene kuti ine ndimakhulupirira Mawu aliwonse. Uthenga uwu uli PAKUTI ATERO AMBUYE. Chimene ine ndimalalikira kapena kuphunzitsa si PAKUTI ATERO AMBUYE, koma chimene Liwu la Mulungu limanena pa matepi CHILI…

Ine ndikudziwa alipo abale ndi alongo amene amati, ndi kumverera, “Ngati inu simukumvera Uthenga wa Branham Tabernacle nsanamira, kuwerenga makalata a Mphungu Zikusonkhana, ndi kumamvetsera mnyumba zanu pa nthawi yomweyo inu simuli Mkwatibwi,” kapena, “Ndi kulakwa kupita ku tchalitchi, inu muyenera kukhala mnyumba mwanu.” NDIKULAKWA KWAMBIRI. Ine sindinayambe ndaganizapo zimenezo, kunena izo, kapena kukhulupirira izo. Izo zapangitsa ngakhale kupatukana kochuluka, zomverera zolimba, ndi kuchotsedwa pakati pa Mkwatibwi ndipo mdani akugwiritsa ntchito izo kuwalekanitsa anthu.

Ine sindikufuna konse kumulekanitsa Mkwatibwi, ine ndikufuna kuti ndimulumikize Mkwatibwi monga Mawu ananenera TIYENERA KUKHALA WOLUMIKIZANA NGATI MMODZI. Ife tisamakangane wina ndi mzake, koma palibenso china mophweka chimene chingatilumikizitse ife koma Liwu la Mulungu pa matepi.

Ife Sitiyenera kumakangana ndikuuza anthu zomwe AYENERA KUCHITA kapena kuti iwo si Mkwatibwi, inuyo ingochitani monga AMBUYE AKUKUTSOGOLERANI. Iwo akali abale ndi alongo athu. Tifunika kukondana ndi kulemekezana.

Tsopano, musakangane. Mwaona? Kupsa mtima kumabweretsa mkwiyo. Chinthu choyamba inu mukudziwa, inu mukukwiyitsa Mzimu Woyera kuchoka kwa inu, inu mudzakhala mukukangana mobwezera. Ndiye Mzimu Woyera umayamba kuwuluka. Kupsa mtima kumabweretsa mkwiyo.

Ndi zimene mneneri ananena apa, ine sindikufuna konse kumvetsa chisoni Mzimu Woyera. Sindikufuna kukangana. Titha kukambirana mwachikondi, koma osati kukangana. Ngati ndalankhula chilichonse chomwe chakhumudwitsa wina aliyense mu zomwe ndalemba kapena kunena, ndikhululukireni, sichinali cholinga changa.

Monga ndanenera kale, ndikumva kuitana pa moyo wanga kuchokera kwa Ambuye kuti ndilole anthu ku Mawu a Mulungu lero. Atumiki ena ali ndi maitanidwe ena ndipo mwina amawona zinthu mosiyana. Utumiki wanga ndi kungomuuza Mkwatibwi kuti, “KUKANIKIZA KUSEWERA” ndi “Liwu la Mulungu pa matepi ndilo Liwu lofunika kwambiri limene mungamve.” “Ine ndikukhulupirira kuti utumiki uyenera kumasewera Liwu la Mulungu pa matepi mu mipingo yawo.”

Makalata amene ine ndimalemba sabata iliyonse ndi a gawo la Mkwatibwi amene amadzimva kuti ali gawo la Branham Tabernacle. Ndikudziwa kuti ena ambiri amawawerenga, koma ndili ndi udindo wochita zomwe ndikumverera kuchitidwa mu tchalitchi chathu. Mpingo uliwonse uli wa pawokha; iwo ayenera kuchita monga iwo akumverera kutsogozedwa ndi Ambuye kuti achite, ndiwo 100% Mawu. Ine Sindikutsutsana nawo iwo, timangosagwirizana. Kwa ine ndi Branham Tabernacle, ife tikungofuna kokha basi kuti tizimva Liwu la Mulungu pa matepi.

Ine Ndimaitana dziko kuti lizijowinana nafe sabata iliyonse. Ndimawalimbikitsa kuti ngati sangathe kujowinana nafe, kusankha tepi, tepi iliyonse, ndikuyikanikiza kuisewera iyo. Iwo adzadzozedwa kuposa kale. Kotero, ine ndikukuitanani inu sabata ino kuti mudzajowinane nafe Lamlungu pa 12:00 P.M., nthawi ya ku Jeffersonville, pamene ife tidzasonkhana pamodzi ndi kumva, 63-0630E Kodi Moyo Wanu Ndi Woyenera Uthenga?

M’bale Joseph Branham

25-0831 Ukulirira Chiyani? Yankhula!

Uthenga: 63-0714M Ukulirira Chiyani? Yankhula!

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mpingo wa Mulungu,

Mulungu analankhula nati, ““Ine sindigwira ntchito pa dziko lapansi, kupatula kupyolera mwa munthu. Ine—Ine—Ine ndine Mpesa; inu ndinu nthambi. Ndipo ine ndimadzifotokoza kokha Inemwini pamene ine ndingakhoze kupeza munthu M’MODZI. Ndipo Ine ndamusankha iye, William Marrion Branham. Ine ndamutumiza iye kumusi kuti adzaitane Mkwatibwi Wanga. Ine ndidzaika Mau anga mu mkamwa mwake . Mau anga adzakhala Mau ake. Iye adzalankhula Mau anga ndi kumalankhula zokhazo zomwe ine ndimalankhula.

Liwu la Lemba linayankhula kupyolera mu Lawi la Moto ndipo linamuuza iye, “Ine ndakusankha iwe, William Branham. Iwe ndi mwamunayo. Ine ndinakulera iwe kwa cholinga ichi. Ine ndidzakutsimikizira iwe mwa zizindikiro ndi zodabwitsa. Iwe ukupita ku dziko la pansi kuti ukaulule Mawu Anga ndi kukamutsogolera Mkwatibwi Wanga. Mawu Anga ayenera kuti akwaniritsidwe ndi IWE.”

Mneneri wathu ankadziwa kuti anatumidwa ndi cholinga chomwecho kuti aulule zinsinsi zonse za Baibulo ndi kutsogolera Mkwatibwi wa Mulungu ku Dziko Lolonjezedwa. Iye ankadziwa chimene iye ananena, Mulungu akanadzalemekeza ndi kuchikwaniritsa. Ine ndikufuna kuti inu musamaiwale Mawu amenewo. Zimene mneneri wathu ananena, Mulungu azilemekeza, chifukwa Mawu a Mulungu anali mwa William Marrion Branham. Iye ali Liwu la Mulungu kwa dziko.

Iye ankadziwa kuti iye anali mngelo wodzozedwa wa Mulungu. Iye ankadziwa mumtima mwake zonse zimene Mulungu ananena zokhudza iye m’Mawu ake. Zomwe zinkamudetsa nkhawa kwambiri zinali zitachitikadi. Iye anali wodzozedwa ndipo ankadziwa kuti iye anali ndi PAKUTI ATERO AMBUYE. Palibe chimene chikanamuletsa kupita kukalankhula Mawu a Mulungu.

Mulungu anamuuza iye, “Mawu Anga, ndi iweyo, Mtumiki Wanga, muli ofanana.” Iye ankadziwa kuti iye ndi amene anasankhidwa kulankhula Mawu osalephera. Ndizo zonse zomwe iye adafunitsitsa. Iye AMATHA KUYANKHUL A, NDIPO MULUNGU ANKACHITITSA ICHO KUKWANILITSIDWA.

Vumbulutso la Uthenga uwu NDI mthenga wa Mulungu wadzoza chikhulupiriro chathu KUPOSA momwe zisanachitikepo mkale lonse. Izo zatisunthira ife mu magulu aakulu kwambiri. Izo zatilekanitsa ife ku chirichonse kupatula Uthenga Wake, Mawu Ake, Liwu Lake, Matepi Ake.

Ziribe kanthu kuti ndife ochepa bwanji, timasekedwa mochuluka bwanji, kunyozedwa, sizimatitekesa mpang’ono pomwe. IFE TIMACHIONA ICHO. IFE TIMAKHULUPIRIRA ICHO. Pali chinachake mkati mwathu. Tinakonzedweratu kuti tidzachiwone ICHO ndipo palibe chimene chidzaatilepheretsa ife kuchikhulupirira ICHO.

Ife timakumbukira zomwe masomphenyawo ananena, “bwerera ukasunge Chakudya”. Kodi nkhokweyo inali kuti? Branham Tabernacle. Kodi pali chirichonse mu dziko, kapena kuzungulira dziko kulikonse, chimene chingafanane ndi Mauthenga amene ife tiri nawo? IWO ndi Liwu lokhalo lotsimikiziridwa ndi Mulungu Mwiniwake kuti liri PAKUTI ATERO AMBUYE. LIWU LOKHALO!

Kodi ndi kutiso kumene ife tikanati, kapena tikanafuna kupita, pamene iye anati;

Apa ndi pomwe Chakudyachi chasungidwira…

Icho chasungidwa pano
Iwo uli pa matepi. Iwo uzipita ku kutambalala konse kwa dziko pa matepi, kumene anthu mu manyumba mwawo. Matepi amenewo azikafika mmanja mwa a okonzedweratu a Mulungu. Iye akhoza kuwalondolera Mawu. Iye alondolera chirichonse ndendende basi mpaka ku ntchito yake. Ndicho chifukwa Iye ananditumiza Ine kuti ndibwerere ndidzachite izi. “Kudzachisunga Chakudyacho kuno.”

Ife Ndife Mkwatibwi wa Mawu Ake Angwiro amene wakhala ndi Chakudya Chake Chosungidwa. Palibe chifukwa chomaliranso, ife timangoyankhula Mawu ndi kupita patsogolo, pakuti ife NDIFE Mawu.

Palibe chomadela nkhawa. Palibeso chifukwa chomakhalira ndi misonkhano ya mapemphero ausiku onse kuti itiwululire kuti ife ndife ndani, Mawu avumbulutsidwa kwa ife. Timadziwa kuti ndife ndani, mofanana ndi mneneri wa Mulungu, ndipo watiuza kale amene anali kupita.

“Mmodzi aliyense wa ife! Kaya ndinu mkazi wa mnyumba, kapena ndinu m—mdzakazi wamng’ono, kapena ndinu mkazi wachikulire, kapena mwamuna wamng’ono, kapena mwamuna wachikulire, kapena chirichonse chimene inu muli, ife tikupita, mulimonse. Sipakhala mmodzi wa ife ati atsalire.” Ameni. “Mmodzi aliyense wa ife akupita, ndipo ife sitiletsa kanthu kalikonse.”

Lankhulani za kutipatsa ife CHIKHULUPILIRO chokwatulitsa!!!

Bwerani mudzajowine gawo la Mkwatibwi wa Mulungu pamene ife tikusonkhana palimodzi mozungulira Liwu lotsimikiziridwa la Mulungu, pamene Iye akuyankhula ndi kutiuza ife: Wokondedwa Wanga, Wosankhidwa Wanga, Mkwatibwi Wanga, Ukulilira Chiyani, Yankhula, ndipo pita patsogolo.

M’bale. Joseph Branham

Uthenga: 63-0714M Ukulilira Chiyani? Yankhula!

Nthawi: 12:00 PM, Nthawi yaku Jeffersonville

Malo:

Koma pali Mpingo weniweni umodzi wokha, ndipo iwe sumajowina Iwo. Iwe umabadwira mwa Iwo. Mwaona? Ndipo ngati iwe wabadwira mwa iwo, Mulungu wamoyo amagwira ntchito Iyemwini kupyolera iwe, ndi kumadzipangitsa Iyemwini kudziwika. Mwaona? Ndiko kumene Mulungu amakhala, mu Mpingo Wake. Mulungu amapita ku Tchalitchi tsiku lirilonse, amakhala moyo mu Mpingo. Iye amakhala moyo mwa inu. Inu ndinu Mpingo Wake. Inu ndinu Mpingo Wake. Inu ndinu Kachisi amene Mulungu amakhalamo. Ndinu Mpingo wa Mulungu wamoyo, inueni.

25-0824 Mgonero

Uthenga: 65-1212 Mgonero

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mawu Otsimikiziridwa Mkwatibwi Yekha,

Ndife othokoza bwanji kwa Mzimu Woyera chifukwa cha Vumbulutso loona la Mawu Ake otsimikiziridwa a lero. Ambiri amadzinenera kuti amakhulupirira M’bale Branham kuti ndi mneneri wa Mulungu amene amakwaniritsa Malemba olonjezedwa a iyemwini, koma Vumbulutso loona la Mawu ndi dongosolo la Mulungu labisika kwa iwo.

Ndi kalata yachikondi iliyonse yomwe Mkwatibwi amamva, Mulungu amatsimikizira kwa ife kuti tili mu Chifuniro Chake changwiro pomvera Njira Yake yoperekedwa ya lero, Liwu la Mulungu pa Matepi.

Ndipo ife tikuyenera kumutsatira Iye, ndiyo njira yokhayo yokhalira nawo Moyo Wamuyaya. Chotero utsogoleri wa Mulungu ndi: kutsatira Mawu otsimikiziridwa a ora mwa Mzimu Woyera.

NJIRA YOKHA yopita ku Moyo Wamuyaya ndi: Mzimu Woyera ukukutsogolerani kuti muzitsatira Mawu otsimikiziridwa. Ndani ali nawo Mawu otsimikiziridwa a lero? Kodi Mulungu anamusankha ndani kuti azitanthauzira Mawu Ake? Kodi Mulungu ananena kuti linali liwu lake la ndani lero? Kodi Mulungu Mwiniwake anati ndani anali mtsogoleri wotsimikiziridwa kuti atsogolere Mkwatibwi Wake lero? Utumiki?

Chimodzimodzi monga ine ndinanena, mphungu yaing’ono pamene iyo inamva Liwu la Mkwati, iyo inapita kwa ilo, odzozedwa, Mawu otsimikiziridwa a Mulungu a tsiku lotsirizali.
Nowa anali Mawu otsimikiziridwa a tsiku lake.
Mose anali Mawu otsimikiziridwa a tsiku lake.
Yohane anali Mawu otsimikiziridwa

Iwo akhoza kupotoza chirichonse kapena kutanthauzira kulikonse kwa Iwo akufuna, koma:
WILLIAM MARRION BRANHAM NDI MAWU OTSIMIKIZIRIDWA A MULUNGU A LERO!!

Chotero utsogoleri wa Mulungu ndi: kutsatira Mawu otsimikiziridwa a ora mwa Mzimu Woyera.

Ndipo kusewera Liwu lotsimikiziridwa la Mulungu mu mpingo wanu si chinthu chofunika kwambiri chimene Mkwatibwi angachite? Ndikofunikira kwambiri kumva liwu losiyana?

Kodi ndi gulu la amuna ndi utumiki wawo umene udzalumikizana ndi kutsogolera Mkwatibwi? Kodi Mkwatibwi adzalumikizidwa ndi zomwe utumiki ukunena? Onse akunena zosiyana, ndiye titsatire ndani?

Kodi kutanthauzira kwawo kwa Uthenga uwu ndi kumene ife tidzaweruzidwa nako? Kodi iwo ali nalo Lawi la Moto likutsimikizira utumiki wawo? Kodi ndiko kutanthauzira kwawo kwa Mawu Mtheradi wanu?

Mneneri anati Mkwatibwi adzakhala WOLUMIKIZANA. Dzifunseni nokha, ndi chiyani chiti chidzachititse uneneri uwu kuti ukwanilitsidwe kuti Ambuye abwere ndi kudzamukwatula Mkwatibwi Wake?

Ndiyeno, pamene anthu a Mulungu ayamba kusonkhananso palimodzi, pamakhala chiyanjano, pamakhala mphamvu. Mukuona? Ndipo paliponse pamene anthu a Mulungu abwera palimodzi kwathunthu, ine ndikukhulupirira chiukitsiro chidzachitika apo ndiye. Padzakhala nthawi ya mkwatulo pamene Mzimu Woyera udzayamba kuwasonkhanitsa iwo. I—iwo adzakhala apang’ono, ndithudi, koma kudzakhala kuli kusonkhana kwakukulu.

Kodi padzakhala kusonkhana kwakukulu kuzungulira utumiki wa munthu wina, kupatulapo mneneri wotsimikiziridwa wa Mulungu? Kodi lidzakhala GULU la atumiki chifukwa ena mwa awutumiki wofutukuka pasanu amanena kuti MUSAMASEWERE LIWU la Mulungu mu tchalitchi mwanu, ndi zolakwika. Kodi iwo adzatsogolera Mkwatibwi ndiye?

CHONDE NDITHANDIZENI! KODI NDI MTUMIKI UTI YEMWE NDIYENERA KUMUTSATIRA POMWE NDIKUFUNA KUKHALA WOLUMIKIDWA NAWO PA PAMSONKHANO WAWUKULU UWO.

Ena amati utumiki wofutukuka pasanu a Mabingu Asanu ndi awiri adzafikitsa Mkwatibwi ku ungwiro . Atumiki ena awutumiki wofutukuka pasanu amati masiku a utumiki wa Munthu Mmodzi atha. Atumiki ena a utumiki wofutukuka pasanu amati ife tiyenera kubwerera ku Pentekosite. Ena amati Uthenga SULI M’theradi. Ena amati ukamasewera matepi ndiwe wokhulupirira milungu. Onse amanena chinachake chosiyana, ndipo ONSE ali ndi matanthauziridwe osiyana, malingaliro osiyana, koma aliyese wa iwo amanena kuti IWO akutsogozedwa ndi Mzimu Woyera.

KODI NDI MTUMIKI WUTI WA UTUMIKI WOFUTUKUKA PASANU YEMWE NDIYENERA KUMUTSATIRA? Bola ngati ine nditsatila abusa “ANGA” awutumiki wofutukuka pasanu, ine ndidzakhala Mkwatibwi? Pali “Magulu” osiyanasiyana a atumiki wofutukuka pasanu. Atumiki 20 awa amasonkhana pamodzi ndi kuchititsa misonkhano yawo, koma 20 amatsutsana kwathunthu ndi azitumiki ena amene akukhala ndi misonkhano yosiyana…ndi misonkhano iti yomwe ine ndipite kuti ndikakhale wangwiro ndi wolumikizana…ena a iwo…onse a iwo?

Ndipo anthu amakhulupilira kuti CHISOKONEZO CHIMENECHI CHILUMIKIZITSA NDIKUMUFIKITSA KU UNGWIRO MKWATIBWI? Onse amati iwo ali Atumiki WOONA AWUTUMIKI WOFUTUKUKA PASANU WOITANIDWA NDI MULUNGU. Koma iwo sakukutsogolerani inu ku UTSOGOLERI WOONA WA MZIMU WOYERA, AKUKUKUTSOGOLERANI INU KWA IWO ENI NDIKU UTUMIKI WAWO.

Kwa ine, simukusowa ngakhale vumbulutso kuti mudziwe zomwe sizingagwirizane kapena kutsogolera Mkwatibwi yense. MAWU OKHA ati adzayanjanitse Mkwatibwi, mwa LIWU LA MULUNGU YEKHA PA MATEPI.

Abale ndi alongo, kulibwino kuti mudzuke ngati mukutsatira m’busa amene akungolalikira ndi kubwereza mawu Mawu, omwe ali odabwitsa ndipo ALI NDENDENDE chimene ayenera kuchita, koma osakuuzani, ndipo chofunika kwambiri, KUCHITA, posewera LIWU LA MULUNGU PA MATEPI MU MPINGO WANU.

M’bale Branham anatiuza kuti:

Tsopano, ife tiri ndi madongosolo Auzimu atatu okha omwe atsalira kwa ife: amodzi a iwo ndi—ndi mgonero, kutsukana-mapazi, ubatizo wa madzi. Ndi zinthu zitatu zokhazo. Ndiwo ungwiro, wa zitatuzo, mwaona.

Ine ndikufuna kuti ife tikhale ndi Chiyanjano cha Mgonero ndi kutsukana Mapazi Lamlungu lino, ngati Ambuye alola. Monga tinachitirapo m’mbuyomu, ndikukulimbikitsani inu kuti muyambe nthawi ya 5:00 PM. Mu nthawi ya m’dera lanu . Ngakhale kuti M’bale Branham ananena kuti atumwi amadya Mgonero nthawi iliyonse imene iwo ankasonkhana, iye ankakonda kuti azidya iwo nthawi yamadzulo, ndipo ankawutchula kuti Mgonero wa Ambuye.

Utumiki wa Uthenga ndi Mgonero udzakhala pa Wailesi ya Liwu, ndipo padzakhalanso ulalo wa fayilo yomwe mungatsitse, kwa iwo omwe sangathe kupeza Wilesi ya Liwu Lamlungu madzulo.

M’bale Joseph Branham

25-0810 Zochitika Zamakono Zimamveka Bwino Ndi Uneneri

Uthenga: 65-1206 Zochitika Zamakono Zimamveka Bwino Ndi Uneneri

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mkwatibwi Woona ndi Wamoyo,

Pamene Yesu, Mawu Iwoeni, anabwera ku dziko lapansi zaka 2000 zapitazo, Iye anabwera monga Iye ananenera kuti Iye akanadzabwera, monga Mneneri. Mawu Ake amalengeza, kuti Iye asanabwere kachiwiri, mawonetseredwe athunthu a Umunthu wa Yesu Khristu adzawonetseredwa kachiwiri mu thupi, mwa mneneri. Mneneri ameneyo wabwera, dzina lake ndi William Marrion Branham.

Kodi wina aliyense angalephere bwanji kuzindikira kuti kumvera Liwu la Mulungu kumalankhula ndi iwo mwachindunji pa matepi kuti ndicho Chifuniro changwiro cha Mulungu? Ife tikudziwa kuti Mawu nthawizonse amadza kwa mneneri Wake; Sizingabwere mwanjira ina iliyonse. Izo ziyenera kubwera kupyolera mu njira ya Mulungu imene Iye anatiwuziratu kale za iyo . Ndi njira yokhayo yomwe Izo zidzadzere konse. Mulungu amayenda mu njira imene Iye analonjeza kuti Iye akanadzachita izo. Iye samalephera konse kuchita izo mwanjira yomweyo yofanana momwe Iye nthawizonse ankachitira.

Wina aliyense wa iwo ankadya chinthu chomwecho, iwo onse ankavina mu Mzimu, iwo onse anali nacho chirichonse mofanana; koma pamene izo zinafika ku nthawi yolekanitsidwa, Mawu ndi omwe analekanitsa. Mmomwe izo zirili lero! Mawu ndi omwe amalekanitsa! Pamene ifika nthawi yake,

Ife tikuwona kuti nthawi ikuchitika tsopano, Mawu akulekanitsa. Mkwatibwi akuimbidwa mlandu wa kuyika zochuluka kwambiri pa mneneri pamene iwo amati, “Pali amuna ena oyitanidwa ndi Mulungu, odzazidwa ndi Mzimu Woyera kuti atsogolere Mkwatibwi lero.” Inu mukusowa zochuluka kuposa matepi okha.Mulungu wayika amuna lero kuti atsogolere mpingo

“Iwe ukuyesera kumaganiza kuti ndiwe mmodzi wekha bwinoko kuposa izo. Ndipo iye anati, “Chabwino, gulu lonseli ndi loyera. Iwe ukuyesera kumadzipanga wekha…” Ngati ife tikanati tinene izo lero, kayankhulidwe ka pa msewu, “Nsangalabwi yokha ya pa doko.”

Ndipo Mose ankadziwa kuti Mulungu anali atamutuma iye uko chifukwa cha izo.

Mulungu ali nawo amuna odzazidwa ndi Mzimu Woyera kuti azitsogolera Mkwatibwi Wake; kuwatsogolera iwo KU PAKUTI ATERO AMBUYE, MNENERI MTHENGA. Pakuti Uthenga ndi m’thenga ali wofanana. Imeneyo ndiyo njira ya Mulungu yosasintha yoperekedwa ya tsiku la lero, ndiponso nthawi zonse.

Chifukwa iwo anamvetsera kwa cholakwika. Pamene Mose, wotsimikizidwira ndi Mulungu, ndi mtsogoleri kuti awasonyeze iwo njira yaku Dziko Lolonjezedwa, ndipo iwo anali atabwera patali chotere bwinobwino, komano iwo sakanakhoza kupitirira limodzi naye.
Tsopano, okhulupirira akhoza kuwaona Iwo, koma osakhulupirira sangakhoze kuwawona Iwo akutsimikizidwira.

Osati kokha kuti inu munasankhidwa kuti mulandire Vumbulutso lalikulu la nthawi yotsiriza ili la lero, koma Mulungu, mwa njira ya matepi Ake a Chakudya chosungidwa, amalankhula pakati pa mizere kwa Mkwatibwi Wake wokoma wa pamtima.

Ndiye ngati inu muli mwana wamwamuna wa Mulungu kapena mwana wamkazi wa Mulungu, inu munali mwa Mulungu nthawiyonseyo. Koma Iye ankadziwa kama wake ndi nthawi yomwe inu mukanati mudzabzalidwe. Kotero tsopano inu mwapangidwa cholengedwa, mwana wamwamuna wa Mulungu, mwana wamwamuna kapena wamkazi wa Mulungu wowonetseredwa kuti mukomane ndi chitsutso cha ora lino kuti mutsimikizitsire Mulungu woona ndi wamoyo wa ora lino, Uthenga umene ukubwerapowu mu nthawi ino. Uko nkulondola! Inu munapangidwa uko asanakhazikitsidwe maziko a dziko.

Ndi kalata yachikondi bwanji yapakati pa mizere kwa Mkwatibwi Wake, ULEMERERO!!! Osati kokha kuti Iye anatidziwa ndi kutisankha ife asanaikidwe maziko a dziko, koma pano Iye akutiuza ife kuti Iye anatisankha ife kuti tikhale ana Ake aamuna ndi aakazi owonetseredwa a LERO. Iye anatiika ife pano pa dziko lapansi lero, pamwamba pa oyera mtima ena onse kuyambira pachiyambi, chifukwa Iye ankadziwa kuti ife tikanati tidzakumane ndi vuto la ora lino kuti titsimikizire Mulungu woona ndi wamoyo wa ora lino, Uthenga umene ukubwera mu nthawi ino.

Ife tinali mwa Mulungu, jini, mawu, chikhumbo kuchokera kuchiyambi, koma TSOPANO Ife tikukhala PAMODZI mu malo Ammwambamwamba mwa Khristu Yesu, kuyankhulana ndi Iye mwa Mawu Ake, kupyolera mu Mawu Ake; pakuti ife NDIFE MAWU AKE, ndipo Iwo akudyetsa miyoyo yathu.

Sitingathe, ndipo sitidzabayilamo kalikonse m’miyoyo yathu koma Mawu osaipitsidwa a Mulungu. Timazindikira ndikukhulupirira kuti ndi njira yoperekedwa ndi Mulungu ya lero.

Ife tikanakonda kuti inu mubwere kuzajowinana nafe Lamlungu lino pa 12:00 p.m., nthawi ya ku Jeffersonville, pamene ife tikumva LIWU LOKHA, Liwu la Mulungu pa matepi, inu mukhoza kunena kuti AMEN kwa Mawu aliwonse omwe inu mumawamva.

M’bale. Joseph Branham

Uthenga: Zochitika Zamakono Zimamveka Bwino Ndi Uneneri 65-1206

Malemba oti muwerenge musanamve Uthenga:

Genesis 22
Deuteronomo 18:15
Masalimo 16:10 / 22:1 / 22:18 / 22:7-8 / 35:11
Yesaya 7:14 / 9:6 / 35:7 / 50:6 / 53:9 / 53:12 / 40:3
Amosi 3:7
Zekariya 11:12; 13:7/14:7
Malaki 3:1/4:5-6
Mateyu woyera 4:4 / 24:24 / 11:1-19
Luka woyera 17:22-30 / 24:13–27
Ahebri 13:8; 1:1
Yohane Woyera 1:1
Chivumbulutso 3:14-21; 10:7

25-0803 Zinthu Zimene Ziti Zidzakakhaleko

Uthenga: 65-1205 Zinthu Zimene Ziti Zidzakakhaleko

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Zikhumbo za Mulungu,

Mawu aliwonse amene analankhulidwa mu Uthenga uwu ndi kalata yachikondi kwa Mkwatibwi Wake. Kuganiza kuti Atate wathu wa Kumwamba amatikonda kwambiri, moti sikuti ankangofuna kuti tiziwerenga Mawu ake, koma ankafuna kuti tizimva Liwu lake likulankhula ku mitima yathu kuti atiuze kuti: “Inu ndinu liwu langa lamoyo, Chikhumbo changa chamoyo, chimene Ine ndingawonetsere pa dziko lapansi.

Ndiyeno kuganiza kuti pambuyo pa nsembe Yake yonse imene Iye anachita pano pa dziko lapansi, moyo umene Iye anakhala, njira imene Iye anayenda. Iye anapempha chinthu chimodzi,

“Kuti kumene Ine ndikakhale, iwonso akakhaleko.” Iye anapempha chiyanjano chathu. Ndicho chinthu chokhacho chimene Iye anawapempha Atate mu pemphero, ubwenzi wanu wosatha.

Kumene ine ndiri, “Mawu Ake,” ifeso tiyenera kukakhalako, kuti tikalandire chiyanjano Chake, Ubwezi Wake Wosatha, kwanthawizonse. Chotero, tiyenera kukhala moyo mwa Mawu aliwonse amene Iye analankhula kwa ife pa matepi kuti tikhale Namwali m’kwatibwi wa mawu, amene amatipanga ife gawo la Mkwati.

Ilo ndilo VUMBULUTSO la Yesu Khristu mu ora lino. Osati chimene Iye anali mu ora lina, yemwe Iye ali TSOPANO. Mawu a lero. Kumene Mulungu ali lero. Ndilo Vumbulutso la lero. Tsopano likukula mwa Mkwatibwi, kutipanga ife mu m’thunthu lokwana la mngwiro la ana aamuna ndi aakazi.

Ife timadziwona tokha mu Mawu Ake. Ife tikudziwa amene ife tili. Ife tikudziwa ife tiri mu dongosolo Lake. Iyi ndi Njira yoperekedwa ndi Mulungu ya lero. Ife tikudziwa Mkwatulo uli pafupi. Posachedwapa okondedwa athu adzawonekera. Kenako tidzadziwa: kuti Ife Tafika. Ife tonse tikupita Kumwamba…inde, Kumwamba, malo enieni monga awa.

Ife tikupita kumalo enieni kumene tizikachitako zinthu, kumene tikakhalako moyo. Ife tizikagwirako ntchito. Ife tikasangalalako. Ife tikakhalako moyo. Ife tikupita ku Moyo, ku Moyo Wamuyaya weniweni. Ife tikupita Kumwamba, paradiso. Chimodzimodzi monga momwe Adamu ndi Eva ankagwirira ntchito, ndi kumakhala moyo, ndi kumadya, ndi kumasangalalako, mmunda wa Edeni tchimo lisanabweremo, ife tiri panjira yathu tikubwerera kumeneko panonso, kulondola, tikubwerera kumeneko. Adamu woyamba, chifukwa cha tchimo, anatichotsako ife. Adamu Wachiwiri, kupyolera mu chirungamo, akutibwezeretsako ife kumeneko kachiwiri; akutilungamitsa ife ndi kutibwezeretsanso ife mmenemo.

Kodi aliyense anganene bwanji za izi pazomwe izo zikutanthauza kwa ife? Chowonadi ndi chakuti tikupita ku paradaiso kumene tikukakhala kwa Muyaya wonse pamodzi. Kulibenso chisoni, zowawa kapena Zokhumudwitsa, ungwiro basi pa ungwiro.

Mitima yathu ikukondwera, miyoyo yathu ili pamoto mkati mwathu. Satana akumayika mochuruka ndi mochuruka zopsinja pa ife tsiku lililonse , koma ife tikusangalalabe. Chifukwa:

  • TIKUDZIWA, YEMWE IFE TILI.
  • TIKUDZIWA, SITINAMULEPHERE, NDIPO SITIDZAMULEPHERA IYE.
  • TIKUDZIWA, TILI MU CHIFUNIRO CHAKE CHANGWIRO.
  • TIKUDZIWA, WATIPATSA IFE VUMBULUTSO LOWONA LA MAWU AKE.

M’bale Joseph, inu mumalemba chinthu chomwecho sabata iliyonse. ULEMERERO, ndidzalemba chimenecho sabata iliyonse chifukwa Iye akufuna kuti inu mudziwe mochuruka momwe Iye amakukonderani inu.Yemwe inu muli. Kumene inu mukupita. Chithunzi chikusandulika kukhala chenicheni. Inu ndinu Mawu mukusandulika kukhala Mawu.

Okondedwa dziko, bwerani mudzajowinane nafe Lamlungu lino pa 12:00 p.m., nthawi ya ku Jeffersonville, polumikizana, osati chifukwa “Ine” ndikukuitanani inu, koma chifukwa “IYE” akukuitanani inu. Osati chifukwa “Ine” ndinatenga tepiyo, koma kumva Mawu ndi gawo la Mkwatibwi kuzungulira dziko lonse nthawi imodzi.

Kodi Ife tingazindikire kuti n’zotheka kuti Mkwatibwi amve Liwu la Mulungu padziko lonse, pa nthawi yofanana? Ameneyo ayenera kukhala Mulungu. Mulungu anali ndi mneneri wake kuti achite izo pamene mngelo Wake anali pano pa dziko lapansi. Iye analimbikitsa Mkwatibwi kulumikizana mu m’pemphero, ONSE PA NTHAWI YOFANANA YA KU JEFFERSONVILLE, 9:00, 12;00, 3:00; Kodi icho ndi chinthu chachikulu motani tsopano, kuti Mkwatibwi akhoza kulumikizana ngati M’MODZI kuti amve Liwu la Mulungu likuyankhula kwa iwo onse pa nthawi imodzi?

M’bale. Joseph Branham

Uthenga: Zinthu Zimene Ziti Zidzakakhaleko 65-1205

Malemba:
Mateyu woyera 22:1-14
Yohane Woyera 14:1-7
Ahebri 7:1-10

25-0727 Mkwatulo

Uthenga: 65-1204 Mkwatulo

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mkwatibwi Wopanda mangawa,
 
 
Ambuye anatipatsa ife nthawi yodabwitsa kwambiri pa msasa sabata yatha pamene Iye anatiululira Mau ake kwa ife. Iye anatsimikizira, mwa Mawu Ake, kuti Mtheradi wathu uli: Mawu Ake, Uthenga uwu, Liwu la Mulungu pa matepi; onse ali ofanana, Yesu Kristu yemweyo dzulo, lero, ndi kunthawi zonse. 
 
Tinamva mmene mdierekezi amayesera kulekanitsa Uthenga kwa mthengayo, koma Ambuye Yesu alemekezeke, Mulungu mwini analankhula kudzera mwa mngelo wake wamphamvu natiuza kuti:

Ife tikupeza apo kuti pamene munthu abwera, atatumidwa kuchokera kwa Mulungu, wodzozedwa ndi Mulungu, ndi PAKUTI ATERO AMBUYE woona, uthenga ndi mtumiki ali mmodzi ndi ofanana. Chifukwa iye watumidwa kuti adzayimire PAKUTI ATERO AMBUYE, Mawu ndi Mawu, kotero iye ndi uthenga wake ali ofanana.

Inu simungakhoze kulekanitsa Uthenga kwa mtumikiyo, iwo ali ofanana, PAKUTI ATERO AMBUYE. Ziribe kanthu zomwe wodzozedwa wabodza aliyense akunena, Mulungu anati iwo ali ofanana ndipo sangalekanitsidwe.
 
Ndiye Iye anatiuza ife kuti sitikusowa chiguduli chosefera kuti tigwire zipumbu zonse pomwe ife tikumvetsera ku matepi, pakuti mulibe nsikidzi kapena madzi a sikidzi mu Uthenga uwu. Ndi chitsime Chake cha kasupe chomwe chimayenda madzi nthawi zonse oyera ndi awukhondo. Nthawizonse akutumphukabe pamwamba, sichimawuma ayi, kumangopitirira kukankhira ndi kukankha, kumatipatsa ife Vumbulutso lochulukira la Mawu Ake.
 
Anatikumbutsa kuti tisaiwale kuti pangano lake ndi ife ndi Losatsutsika, Losatsutsika, koma koposa zonse, Lopanda mangawa.
 
Kaya ndi chikondi, chithandizo, kapena kugonja, ngati china chake chopanda mangawa ndi MTHERADI ndipo sichigwirizana ndi mfundo kapena zikhalidwe zina zapadera: izo zichitika zivute zitani.
 
 Ndiye Iye anafuna kukhomerera msomali, kotero anatiuza ife kuti lero Malemba Ake akukwaniritsidwa pamaso pathu.

Kuti d-z-u-w-a lomwelo limene limatuluka kummawa ndi d-z-u-w-a lomwelo limene limadzalowa kumadzulo. Ndipo M-w-a-n-a wa Mulungu yemweyo amene anabwera kummawa ndi kudzadzitsimikizira Yekha ngati Mulungu wowonetseredwa mu thupi, ndi M-w-a-n-a wa Mulungu yemweyo kumadzulo kwa dziko lapansi kuno, amene akudzizindikiritsa Yekha pakati pa mpingo usikuuno, yemweyo dzulo, lero, ndi kwanthawizonse. Kuwala kwa kumadzulo kwa Mwana kwafika. Lero Lemba ili lakwaniritsidwa pamaso pathu.

 Mwana wa Munthu wabweranso mu thupi laumunthu mu tsiku lathu, monga momwe Iye analonjezera kuti Iye akanadzatero, kuti adzaitane Mkwatibwi. Ndi Yesu Khristu akuyankhula molunjika kwa ife, ndipo Izo sizikusowa kutanthauzira kwa munthu. Zonse zomwe tikusowa, zomwe tikufuna, ndi Liwu la Mulungu loyankhula pa tepi lochokera kwa Mulungu Mwiniwake.

Ndi vumbulutso la kukwaniritsika kwa Mawu kukhalitsidwa owona. Ndipo ife tikukhala mu tsiku limenelo. Mulungu alemekezeke! Vumbulutso la chinsinsi la Iyemwini.

Ndi nthawi yaulemerero bwanji yomwe Mkwatibwi ali nayo, ali mu kukhalapo kwa Mwana, akucha. Tirigu wabwereranso ku tirigu, ndipo palibe chotupitsa pakati pathu. Liwu loyera la Mulungu loyankhula kwa ife, kutiumba ndi kutipanga ife mu chifaniziro cha Khristu, Mawu.
 
 
Ife ndife ana aamuna ndi aakazi a Mulungu, chikhumbo Chake chimene Iye anachikonzeratu kuti chibwere mu m’badwo uno, m’badwo waukulu kwambiri mu mbiriyakale ya dziko.  Iye ankadziwa kuti ife sitikanati tilephere, ife sitikanati tinyengerere, koma ife tikanakhala Mkwatibwi Wake wa Mawu owona ndi wokhulupirika, Mbewu Yake Yachifumu yolonjezedwa Yapamwamba ya Abrahamu yomwe inali nkudza.
 
Mkwatulo uli pafupi. Nthawi yafika kumapeto. Iye akudzera Mkwatibwi Wake yemwe wadzikonzekeretsa Yekha koma akukhala mu Kukhalapo kwa Mwana, akumva Liwu Lake kumuveka Mkwatibwi Wake. Posachedwapa tidzayamba kuona okondedwa athu omwe ali kuseri kwa ketani ya nthawi, omwe akuyembekezera ndi kulakalaka kukhala nafe.

Matepi ndi njira yoperekedwa ndi Mulungu kuti afikitse Mkwatibwi Wake ku ungwiro. Matepi awa ali chinthu chokha chimene chidzagwirizanitsa Mkwatibwi Wake. Matepi awa ali Liwu la Mulungu kwa Mkwatibwi Wake.
 
Ine ndikukuitanani inu kuti mubwere ndi kudzalumikizana nafe, gawo la Mkwatibwi Wake, Lamlungu lino pa 12:00 p.m., nthawi ya ku Jeffersonville, pamene ife tikumva zonse za zomwe zikukonzekera kuti zichitike posachedwapa: Mkwatulo 65-1204. 

 
M’bale. Joseph Branham