All posts by admin5

25-1228 Kuzindikira Tsiku Lanu Ndi Uthenga Wake

Uthenga: 64-0726M Kuzindikira Tsiku Lanu Ndi Uthenga Wake

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mkwatibwi Wodulidwa,

Lero lino, mpingo wayiwala mneneri wawo. Iwo Samufunanso Iye mpang’ono pomwe kuti azilalikira m’matchalitchi awo. Iwo amanena kuti ali ndi abusa awo kuti aziwalalikira iwo ndi kumatchula mobwereza mawu ndi kumasulira Mawu. Kulalikira n’kofunika kwambiri kuposa kumvetsera liwu la Mulungu pa matepi m’matchalitchi awo.

Koma Mulungu Iye ankadziwa kuti ankayenera kukhala ndi mneneri Wake; mmenemu ndi momwe nthawi zonse Iye amaitanira ndi kutsogolera Mkwatibwi Wake. Iye anatidula kuchokera m’mitundu yonse ndi Lupanga Lake lakuthwa konsekonse, Mzimu Wake Woyera, Liwu Lake loyankhulidwa ndi mneneri Wake.

Iye watidula ife ndi Liwu limenelo. Ndicho chifukwa chake Iye analijambula ilo ndi kuliyika pa tepi. Mwa Vumbulutso ife timawona momwe Malemba alili angwiro! Mkwatibwi sangache pokhapokha Mwana atamuchetsa iye.

Ziribe kanthu ndi mochuluka bwanji momwe inu mungalalikire, chirichonse chimene inu mungachite, icho sichingakhoze kucha, icho sichingawonetseredwe, icho sichingatsimikiziridwe; kokha ndi Iye Amene anati, “Ine ndine Kuwala kwa dziko lapansi,” Mawu.

Mawu adatiuza ife kuti Mzimu Woyera mwiniwake adzabweranso ndi kudzatichetsa ife, kudzatsimikizira, kudzasonyeza umboni ndi kudzadzipanga Iyemwini kudzadziwonetsera. Kuwala kwamadzulo kwafika. Mulungu akudzionetsera yekha mu thupi kuti ayitane Mkwatibwi Wake.

Iye ndiye amene wakuitanani INU ndi Mzimu Wake Woyera, Mawu Ake, Liwu lake. Iye ndiye amene anakusankhani INU. Iye ndiye amene akukuphunzitsani INU. Iye ndiye amene akutsogolerani INU. Ndi chiyani? Mzimu Wake Woyera, Liwu Lake likuyankhula MWACHINDUNJI KWA INU.

Koma izo ndi zakale kwambiri kwa iwo lero lino. Iwo sangakhoze kusewera matepi m’matchalitchi awo. Iwo Sakuzindikira. Ndicho chifukwa chake ali mu mkhalidwe womwe ali. Koma kwa inu, izo zawululidwa kuti ndi njira yoperekedwa ndi Mulungu, IZO NDI PAKUTI ATERO AMBUYE KWA INU.

Chotero pakuyenera kubwera a—a—a Mphamvu, Mzimu Woyera Mwiniwake, kuti udzachetse, kapena kutsimikizira, kapena kudzatsimikizira, kapena kudzawonetsera icho chimene Iye ananeneratu kuti chikanadzachitika mu tsiku lino. Kuwala kwa kumadzulo kukupanga zimenezo. Ndi nthawi yotani!

Ife ndife Mkwatibwi wangwiro wa Mawu a Mulungu amene mneneri wake anaona mu masomphenya. Ife ndiwo amene Iye anatumiziridwako mneneri wake kuti awaitane ndi Mawu ake, ndipo iwo tsopano akukhala ndi CHITSITSIMUTSO, chifukwa tsopano ife tikudziwa chimene ife tiri.

Kutsitsimutsa, apo, ndi mawu omwewo amene amagwiritsidwa ntchito kwina kulikonse, ine ndinangowayang’ana iwo, amatanthauza, “chitsitsimutso.” “Iye adzatitsitsimutsa ife akadzatha masiku awiri.” Izo zidzakhala, “Patsiku lachitatu Iye adzatitsitsimutsanso ife, Iye atatibalalitsa ife, ndi kutichititsa khungu, ndi kuting’amba ife.”

Atate anatuma mneneri wake kuti ayang’anire Mkwatibwi wake kuti tisachoke pa mzere. Kumbukirani, awa anali masomphenya!

Mkwatibwi anadutsa malo omwewo amene Iye anali pamene Iye anali pachiyambi. Koma ine ndinali kumuwona Iye akuchoka pa sitepe, ndi kumayesera kumukokera Iye mmbuyo.

Koma kodi “iye” angamukokere m’mbuyo bwanji lero? “Iye”, mwamunayo, sali pano padziko lapansi. NDI MAWU! Kodi Mawu OKHA Otsimikiziridwa a lero ndi ati? Liwu la Mulungu pa matepi.

Atumiki ai oyitanidwa kulalikira Mawu potchula mobwera zomwe mneneriyo ananena. Malinga ndi mneneri mwiniwake, iwo sayenera kunena china chilichonse mochuluka

Zoonadi, aIi oyitanidwa kuphunzitsa ndi kulalikira Mawu amenewo. Koma pali LIWU LIMODZI LOKHA LOMWE NDILOTSIMIKIZIRIDWA NDI MULUNGU IYEMWINI KUTI NDILO PAKUTI ATERO AMBUYE.

Chotero ine ndikunena, mu Dzina la Yesu Khristu! Musati inu muwonjezere kanthu kamodzi. Musati mutenge, kuyika malingaliro anu omwe mwa Iwo. Inu muzingonena chimene chikunenedwa pa matepi awo. Inu muzingochita chimodzimodzi chimene Ambuye Mulungu wakulamulirani kuti muchite. Musati muwonjezere kwa Iwo.

Ngati inu munena kuti “ameni” pa mawu aliwonse amene m’busa wanu kapena mtumiki wanu akunena, inu mwatayika. Koma ngati munena kuti “AMENI” PA MAWU ALIWONSE AMENE MULUNGU ANAYANKHULA KUDZERA MWA MNENERI WAKE PA MATEPI, INU NDINU MKWATIBWI NDIPO MUDZAKHALA NDI MOYO WOSATHA.

Mneneri wa Mulungu anali munthu amene Mulungu anasankha kulankhula kudzera mwa iye. Kunali kusankha Kwa Mulungu kumugwiritsa ntchito iye kulankhula Mawu Ake ndikuwayika pa matepi kuti Mkwatibwi nthawi zonse akhale ndi PAKUTI ATERO AMBUYE WOTI AZIMVERA.

Iye sakufuna kuti Mkwatibwi Wake azidalira zomwe anthu ena akunena, kapena kutanthauzira kwawo Kwa Mawu Ake. Iye akufuna kuti Mkwatibwi Wake azimva kuchokera pakamwa pake kupita m’makutu mwawo. Iye sakufuna kuti Mkwatibwi Wake azidalira wina aliyense koma Iyemwini.

Ife tikadzuka m’mawa, timakonda iye kuti atiuze ife kuti, “Mmawa wabwino abwenzi. Ine Ndilankhula ndi inu lero ndikukuuzani momwe ine ndimakukonderani inu komanso momwe inu ndi ine tili AMODZI. Ndili ndi ambiri omwe ndidzawapatse moyo wosatha, koma INU nokha ndinu Mkwatibwi wanga wogwiridwa pa dzanja. INU nokha ndi amene ine ndapereka Vumbulutso maziko adziko asanakhazikitsidwe .

Ambiri amakonda kundimva, koma ine ndakusankhani inu kuti mukhale Mkwatibwi Wanga. Pakuti mwandizindikira Ine ndipo mwakhala ndi Mawu Anga. Inu Simunanyengerere, simunasewere, koma mwakhalabe okhulupirika ndi Mawu Anga.

Nthawi yayandikira. Ndikubwera kudzakutengani posachedwa. Choyamba, mudzawona omwe ali kale ndi ine tsopano. O, momwe iwo akufunira kukuonani inu ndikukhala nanu. Musadandaule ana aang’ono, chilichonse chili pa nthawi yake, basi pitirizani kumenyera.”

Monga mtumiki wa Uthenga, ine sindingathe kuwona chinthu chimodzi chatsalira koma kupita kwa Mkwatibwi.

M’bale Joseph Branham

Uthenga: 64-0726M “Kulizindikira Tsiku Lanu ndi Uthenga Wake”
Nthawi: 12:00 P.M., nthawi ya ku Jeffersonville

Malemba oti muwerenge musanamve Uthenga:
Hoseya: Chaputala 6
Ezekieli: Chaputala 37
Malaki: 3:1 / 4:5-6
II Timoteo: 3:1-9
Chivumbulutso: Chaputala 11

25-1221 Kupita Kuseri Kwa Msasa

Uthenga: 64-0719E Kupita Kuseri Kwa Msasa

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Wachikondi,

Mulungu samasintha. Mawu Ake samasintha. Pulogalamu yake simasintha. Ndipo Mkwatibwi Wake samasintha, Ife tidzakhala ndi Mawu. Iwo ndi oposa moyo kwa ife; iwo ndi Kasupe wa Madzi amoyo.

Chinthu chokha chomwe ife tapatsidwa ntchito ndikumva Mawu, omwe ndi Mawu a Mulungu otsimikiziridwa omwe adajambulidwa ndikuyikidwa pa matepi. Chinthu chokha chomwe timawona si chikhulupiriro, osati gulu la amuna, sitiwona china chilichonse koma Yesu, ndipo Iye ndiye Mawu opangidwa kukhala thupi mu masiku athu ano.

Mulungu ali mu Msasa wathu ndipo tili panjira yopita ku Ulemerero motsogozedwa ndi Lawi la Moto, lomwe ndi Mulungu Mwiniwake akulankhula kudzera mwa mneneri wake wotsimikiziridwa wa Malaki 4. Tikudya Mana wobisika, Madzi amoyo omwe Mkwatibwi yekha ndi amene angadye.

Mulungu sasintha njira zake, koteroso mdierekezi sasintha njira zake. Zimene adachita zaka 2000 zapitazo, akuchita zomwezo lero, kupatula kuti ali wa mphavu kwambiri.

Tsopano, zitatha zaka foro handiredi, Mulungu anadzayenda kumene pakati pawo tsiku lina. Molingana ndi Lemba, Iye anali woti adzasandulike thupi ndi kudzakhala pakati pawo. “Dzina Lake azidzatchedwa Wauphungu, Kalonga wa Mtendere, Mulungu Wamphamvu, Atate Wosatha.”
Ndipo pamene Iye anadzabwera pakati pa anthuwo, iwo anati, “Ife sitimulola kuti Munthu uyu azitilamulira ife!

Potengela ndi Malemba, Mwana wa Munthu adzabweranso ndi kukhala ndi moyo ndi kudziulula Yekha mu thupi la munthu, ndipo Iye anachitadi zimenezo, ndipo iwo akunena zomwezo. Inde, iwo amakamba mobwereza ndi kulalikira Uthenga, koma Iwo samalola munthu ameneyo kuwalamulira iwo.

Izi ndizo kwenikweni zomwe zili kuchitika :

Ndipo monga zinaliri kumeneko, chomwechonso izo ziri tsopano! Baibulo linati mpingo wa Laodikaya ukanadzamuika Iye panja, ndipo Iye anali akugogoda, akuyesera kuti alowe mkati. Pali chinachake cholakwika penapake.
Tsopano, bwanji? Iwo anali atapanga msasa wawo wawo.

Munthu anganene kuti, “Ine ndikudziwa ndipo ine ndimakhulupirira kuti M’bale Branham anali mneneri. Iye anali mngelo wachisanu ndi chiwiri. Iye anali Eliya. Timakhulupirira Uthenga uwu. Kenako iye ndikupanga mtundu wina wakunyozela, Iwo angakhale uliwonse womwe ulipo, osasewera Liwu LOKHA LOTSIMIKIZILIDWA la Mulungu mu mpingo wawo… Pamenepo pali chinachake cholakwika penakwake. Tsopano, ndi chifukwa chiyani? Iwo adapanga msasa wawo.

Ine ndikunena zinthu izi kuti osati kuti tilekanitse mpingo iyayi, Mawu a Mulungu ndi emene amachita zimenezo. Ine ndikufuna kuti ife tonse tigwirizane pamodzi, tikhale CHINTHU CHIMODZI wina ndi mnzake komanso ndi Iye, koma pali njira imodzi yokha yochitira zimenezo: mozungulira Liwu la Mulungu pa matepi. Ameneyo ndiye PAKUTI ATERO AMBUYE YEKHA WA MULUNGU.

Mulungu wavumbulutsira njira Yake yangwiro kwa ife. Iyo ili yaulemerero kwambiri ndiposo yosavuta. Uthenga uliwonse umene timamumva Iye akutiuza, kutitsimikizira, kutilimbikitsa, kuti NDIFE MKWATIBWI WAKE. Tili mu chifuniro Chake changwiro. Tadzipanga ife eni kudzikonzekeretsa tokha pa KUMUNVA IYE

Uthenga uwu uli watsopano kwambiri kuposa nyuzipepala ya mawa. Ndife ulosi womwe ukukwaniritsidwa. Ndife Mawu owonetseredwa. Mulungu amatitsimikizira ndi Uthenga uliwonse umene timamva kuti tsiku ili lero , Lemba ili likukwaniritsidwa.

Pakhoza kukhala ena uko kudutsa mafuko, kuzungulira dziko, amene ngakhale tepi iyi idzakawapeza mmakomo mwawo kapena mmatchalitchi mwawo. Ife tikupemphera, Ambuye, kuti pamene msonkhano ukupitirira, pa—pa…kapena tepiyo izikaseweredwa, kapena pamalo amene tingadzakhale tiripo, ka—kapena chikhalidwe, mulole Mulungu wamkulu wa Kumwamba mulemekeze kudzipereka uku kwa mitima yathu mmawa uno, ndipo muchiritse osowa, mupereke kwa iwo zimene iwo akuzisowa.

Dikirani chabe mwa ka mphindi ….Kodi Liwu la Mulungu kwa dziko lapansi linalosela ndi kunena chiyani?….anthu azizasewera matepi m’nyumba zawo kapena m’matchalitchi awo.

Koma ife tikutsutsidwa ndi kudzudzulidwa ponena kuti ife SITINGAKHALE NDI Tchalitchi cha Tepi Cha mnyumba? Kodi M’bale Branham sananenepo kuti muzisewera matepi m’matchalitchi anu?

ULEMERERO KWA MULUNGU, IMVETSENI IYO, WERENGENI IZO, IZO NDI PAKUTI ATERO AMBUYE. Ndipo sikuti Iye anangonena izi zokha, komanso posewera matepi m’nyumba zanu ndi m’matchalitchi, Mulungu wamkulu wa Kumwamba adzalemekeza kukhulupirika kwa mitima yathu ndikuchiritsa osowa ndikutipatsa ife CHILI CHONSE CHOMWE TIKUFUNA!!

Chobwerezedwa ichi chimodzi chokhachi CHIKUTSIMIKIZIRA kuti anthu akumvetsera abusa awo ndipo iwo SAKUMVA MAWU, kapena Iwo angawatsutse ndikuwatsimikizira ndi MAWU kuti ife tili mu CHIFUNIRO CHAKE CHANGWIRO, ndipo ndi CHIFUNIRO CHAKE CHANGWIRO KUSEWERA MATEPI M’MATCHALITCHI AWO.

Sindikusokeretsa kapena kubwereza mawu molakwika Mawu monga momwe ambiri amanenera. Imvereni ndipo muwerenge izo nokha.

Ndipo ndi zophweka komanso zangwiro, INGOKANIKIZANI KUSEWERA ndipo mumve Liwu la Mulungu likulankhula nanu. Nenani “Amen” ku Mawu aliwonse omwe inu mukumva. Inu Simuyenera konse kuwamvetsa, inu muyenera kokha kungokhulupilira izo.

“Ine ndikufuna kuti ndipite opanda msasa. Ziribe kanthu kuti ine ndilipira chiyani, ine nditenga mtanda wanga ndipo ndiziunyamula iwo tsiku ndi tsiku. Ine ndipita mopitirira msasa. Ziribe kanthu kuti anthu azinena chiyani za ine, ine ndikufuna kuti ndizimutsatira Iye kunja kwa msasa. Ine ndakonzeka kuti ndizipita.”

Bwerani ndipo mudzapite mopitilira chotchinga cha mawu kupita ku Mawu a Mulungu Lamlungu lino nthawi ya 12:00 PM, nthawi ya ku Jeffersonville. Izo zilibe malire zomwe Mulungu angachite ndiso zomwe adzachita ndi munthu amene ali wokonzeka kupita mopitirira msasa wa anthu.

M’bale Joseph Branham

Uthenga: 64-0719E Kupita Mopitilira Msasa

Malemba Opatulika: Ahebri 13:10-14 / Mateyu 17:4-8

25-1214 Phwando La Malipenga

Uthenga: 64-0719M Phwando La Malipenga

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mkwatibwi Wangwiro

Izi sizongozipanga, abwenzi. Izi ndi PAKUTI ATERO AMBUYE, Lemba.

Mkristu aliyense amafuna kukhala Mkwatibwi, koma tikudziwa kuti Mkwatibwi Wake adzakhala okhawo osankhidwa ake ochepa . Tikudziwa kuti Iye ali ndi chifuniro chongololera, koma Mkwatibwi Wake ayenera kukhala mu chifuniro chake changwiro. Kotero, ife tiyenera kufunafuna Mulungu mu Mawu Ake, ndipo kenako mwa vumbulutso, ife tidzadziwa chifuniro Cha Iye changwiro momwe ife tingakhalire Mkwatibwi Wake.

Ife tiyenera kufufuza lemba, chifukwa tikudziwa kuti Mulungu SAMASINTHA malingaliro Ake pa Mawu Ake. Mulungu sasintha pologaramu yake.Iye Sasintha CHILICHONSE. Momwe Iye anachitira izo nthawi yoyamba ndi wangwiro. Zimene Iye anachita dzulo Adzachitanso chimodzimodzi lero.

Momwe Iye anapulumutsira munthu kuyambira pachiyambi, Iye ayenera kupulumutsa munthu lero mwanjira yomweyo. Momwe Iye Anachiritsira munthu woyamba, Iye ayenera kuchita chimodzimodzi lero. Momwe Mulungu anasankhira kuyitana ndi kutsogolera Mkwatibwi Wake, Iye Adzachita chimodzimodzi lero; pakuti Iye ndi Mulungu ndipo sangasinthe. Mawu amatiuza kuti Yesu Khristu ali YEMWEYO dzulo, lero ndi kwanthawi zonse.

Kotero, Ife tikamawerenga Mawu Ake, timatha kuona bwino lomwe momwe Iye anasankhira kuyitana ndi kutsogolera Mkwatibwi Wake pa nthawi iliyonse. Adasankha MUNTHU MMODZI. Iye anati iwo anali Mawu a tsiku lawo. Mneneri anatiuza Ife kuti Iye SANALI ndi gulu la amuna; Iwo amakhala ndi njira zosiyanasiyana, malingaliro osiyanasiyana, ndipo chofunika kwambiri, Iye anati, MAWU A MULUNGU SAMAFUNIKA KUTANTHAUZIRA.

Ndiye, zomwe mneneri aliyense adalankhula mu mbadyo uliwonse sizingawonjezeredwepo kapena kuchotseredwapo. Ziyenera kukhala Mawu pa Mawu zomwe IYE ANALANKHULA. Zophweka kwambiri ngati Inu mundifunsa ine kuti nanga njira yoperekedwa ndi Mulungu ndi iti….KHALANI NDI MNENERI.

Tsopano, ife sitikungodziwa kokha kwenikweni yomwe yakhala ili njira yoperekedwa ndi Mulungu kuyambira pachiyambi, Ambuye adzalankhula ngakhale kudzera mwa mngelo wake ndikutiuza zomwe Iye adzachita mtsogolo, kuti basi adzatsimikizire kachiwiri, MULUNGU SAMASINTHA DONGOSOLO LAKE.

Mkwatibwi Wake (ife) titachoka padziko lapansi lino ndikuyitanidwa ku Mgonero wa Ukwati, kodi Mulungu adzaitana bwanji Ayuda osankhidwa 144,000? Gulu la amuna?

Ndipo pa nthawi yomweyo…Tsopano, mwamsanga pamene Mpingo uwu (Mkwatibwi) ukusendezedwa pamodzi, Iwo ukutengedwera mmwamba; ndipo chinsinsi icho cha Chisindikizo cha Chisanu ndi chiwiri, kapena Chisindikizo cha Chisanu ndi chiwiri, chinsinsi cha kupita. Ndipo Ayuda akuitanidwa ndi chinsinsi cha Lipenga la Chisanu ndi chiwiri, chimene chiri aneneri awiri, Eliya ndi Mose, ndipo iwo akubwereranso.

Kotero Mkwatibwi akusendezedwa pamodzi, ife tidzatengedwera mmwamba. Ife Tikudziwa kuti pali chinthu chimodzi chokha chomwe chingamusendeze Mkwatibwi pamodzi, Mzimu Woyera, ndipo Mzimu Woyera ndi Mawu Ake, ndipo Mawu Ake a lero ndi Liwu la Mulungu, ndipo Liwu la Mulungu ndi…

Ngati ine ndidakukhumudwitsani Inu pa kunena zimenezo, mundikhululukire ine, koma, ndinaverera kuti mwina icho chidazembedwa, koma, Ine ndine Liwu la Mulungu kwa inu. Mukuona? Ine Ndikunenanso zimenezo kachiwiri, nthawi imene ija ndidali pansi pa kudzoza, Inu mukuona.

Ndingolankhula ine pomwe pano ndi kunena kuti, CHOBWEREZA CHIMODZI chokha ichi chochokera kwa mthenga wa mngelo wotsimikiziridwa wa Mulungu chiyenera kukhala chokwanira kwa onse odzitcha okhulupirira mu Uthenga wa nthawi yotsiriza uwu kuti apemphe abusa awo kuti azikanikiza kusewera m’matchalitchi awo kapena kuti achoke pa udindo kuti iwo asankhe m’busa wokhala ndi VUMBULUTSO LENI LENI LOCHOKERA KWA MULUNGU.

Choncho, Lipenga linamveka ndipo aneneri awiri awa akuwonekera chifukwa Iye sangakhale ndi mngelo wake wachisanu ndi chiwiri ndi Mkwatibwi wake pano padziko lapansi nthawi yomweyo yomwe akubwera. Ndiye kodi Iye akuwayitani bwanji Ayuda? Mwanjira yofanana momwe Iye anamuyitanila Mkwatibwi wake wa Amitundu.

Ndipo Ayuda akuitanidwa ndi chinsinsi cha Lipenga Lachisanu ndi chiwiri, chomwe ndi aneneri awiri…

Mkwatibwi ayenera kuti achokepo pa njirayo, kuti azipita mmwamba tsopano; kuti antchito awiriwo, antchito awiri awo a Mulungu, mu Chivumbulutso, aneneri awiriwo, akhoza kuwonekera poyera, kuti adzawombe Lipenga la Chisanu ndi chiwiri kwa iwo, kumudzindikiritsa kwa iwo Khristu.

Zomveka bwino kwambiri, Mulungu sasintha dongosolo lake.Iye anatumiza aneneri Ake. Motero, Mkwatibwi Wake adzakhala ndi njira Yake yoperekedwa, mneneri Wake wa angelo, Liwu la Mulungu pa matepi.

Kenako kuti izo zimveke bwino, Mulungu kachiwiri akulankhulanso ndikumuuza Mkwatibwi Wake kuti: Mwakhala okhulupirika kwa Ine ndi njira Yanga yoperekedwa, kotero njira Yanga yoperekedwa ya tsiku lanu idzayankhula kwa inu:

Mngelo wachisanu ndi chiwiri, mtumiki, akuti, “Taonani Mwanawankhosa wa Mulungu amene akuchotsa tchimo la dziko lapansi!”

Kotero lofunikira kwambiri ndi LIWU LIMENELO; LIWU LA MULUNGU akulankhula kudzera mwa mngelo wake wachisanu ndi chiwiri pa matepi. Mulungu adzagwiritsa ntchito MAWU AMENEWO, LIWU LA M’NGELO WAKE WACHISANU NDI CHIWIRI. OSATI GULU…OSATI INE…OSATI M’BUSA WANU…LIWU LA MTUMIKI WAKE WA MNGELO WACHISANU NDI CHIWIRI kuti atidziwitse ife kwa Iye, Ambuye wathu Yesu Khristu.

Motero, ife tikudziwa:

• IFE NDIFE MKWATIBWI WAKE.
• IFE TILI MU CHIFUNIRO CHAKE CHANGWIRO.
• IFE TIKUTSATIRA DONGOSOLO LAKE LA TSIKU LA LERO PAKUKANIKUZA KUSEWERA.

Gawo la Mkwatibwi Wake lidzakhala likusonkhana Lamlungu lino nthawi ya 12:00 PM, nthawi ya ku Jeffersonville, kumvetsera m’busa wathu, mthenga wa mngelo wa Mulungu, William Marrion Branham, ndipo Iye adzalankhula ndi kutiululira kuti palibe mpingo wina, palibe gulu lina la anthu kuyambira chikhazikitsidwire kwa dziko lapansi, lomwe lakhala ndi mwayi woti ife tigwirizane pamodzi kumvetsera Mulungu akulankhula mwachindunji ndi iwo.

Ndi anthu odala bwanji ife. Ife Ndi okondwa kwambiri. Ife kotero ndi oyamikira kwambiri . Mkwatibwi akukhala MMODZI ndi Mkwati.

M’bale Joseph Branham

Uthenga: Malipenga A Phwando 64-0719M.

Malemba oti muwerenge musanamve Uthenga:

Levitiko 16
Levitiko 23:23-27
Yesaya 18:1-3
Yesaya 27:12-13
Chivumbulutso 10:1-7
Chivumbulutso 9:13-14
Chivumbulutso 17:8

25-1207 Kenako Yesu Anabwera Ndipo Anadzaitana

Uthenga: 64-0213 Kenako Yesu Anabwera Ndipo Anadzaitana

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mkwatibwi wa Mawu,

Tikukhala mu nthawi yamdima kwambiri, koma tilibe MANTHA, Ambuye wabwera. Wabwera kudzakwaniritsa Mawu Ake mu tsiku lomaliza. Chimene Iye anali panthawiyo, Iye ali lero. Chimene kuonekera kwake ndi kudziwika kwake zinali, ndi lero. Iye akadali Mawu a Mulungu, akudziwonetsera Yekha mu thupi la munthu mwa mngelo wake wachisanu ndi chiwiri wamphamvu ndipo watiululila ife, ife ndife Mkwatibwi wake wa Mawu a moyo.

Tilibe nthawi ya mtsutso kapena mkangano; Ife tinadutsa tsiku limenelo; tikupita patsogolo, Ife tikuyenera kukafika kumeneko. Mzimu Woyera wabwera pakati pathu. Ambuye Yesu mu mawonekedwe a Mzimu wadziulula ndi kudziwonetsera Yekha kudzera mwa mneneri Wake kuti Iye ndi Liwu la Mulungu kwa Mkwatibwi Wake.

Iye anati adzabwera. Iye anati adzachita izi. Iye anati adzauka m’masiku otsiriza ndikuchita zinthu izi monga momwe Iye anachitira pamene anabwera m’thupi nthawi yoyamba, ndipo apa akuchita izi. Kodi inu mukuopa chiyani? PALIBE!!!

Tili pa njira ya kwathu yopita ku Ulemerero! Palibe chomwe ife chingatilepheretse. Mulungu adzatsimikizira Mawu Ake. Sindikusamala zomwe zikuchitika. Nthawi yafika yochitapo kanthu. Nthawi yafika yo khulupilira kapena kusakhulupirira. Mzere uja wolekanitsa umene umabwera kwa mwamuna ndi mkazi aliyense wafika.

Inu Munabadwira pa cholinga. Pamene Kuwala kunakukanthani inu, Kunachotsa kudetsedwa konse mkati mwa inu. Pamene munamva Liwu Lake likulankhula ndi inu pa matepi, chinachake chinachitika. Kunalankhula ndi moyo wanu. Kunati, “Ambuye wabwera ndipo akukuitanani inu. Musatope, musaope, Ine ndikukuitanani inu. Ndinu Mkwatibwi Wanga”.

Oh Anthu inu, onetsetsani! Musamangotenga chatheka chilichose pa izo. Mulungu ali ndi pologaramu: Mawu Ake Iye adawajambula pa matepi. Ambuye wabwera ndipo akukuitanani inu. Bwerani ku njira yoperekedwa ndi Mulungu.

Ambuye adzagwirizanitsanso Mkwatibwi Wake padziko lonse lapansi ndi Liwu Lake. Adzatilimbikitsa ife, kutitsimikizira ife, kutichiritsa ife, kutibweretsa mu mKukhalapo Kwake kwamphamvu ndikutiuza ife:

Mbuye wabwera ndipo Iye akuitana iwe. Oh, wochimwa, oh, munthu wodwala, kodi iwe sukuwona Mbuye akuwonetseredwa mwa anthu, pakati pa okhulupirira? Iye wabwera kuti adzaitane ana Ake okhulupirira kuti akhale athanzi. Iye wabwera kuti adzamuitanire wochimwa ku kulapa. Wobwerera mmbuyo, membala wa mpingo, Mbuye wabwera ndipo akukuitanani inu.

Kodi ndikutsanyulila kotani Kwa mzimu woyera komwe mkwatibwi adzakhale nako Lamlungu lino pamene Mulungu akusonkhanitsaso ana ake pamodzi kachiwiri ndi kulowa m’nyumba zathu, m’matchalitchi athu, m’misonkhano yathu, ndikutiyitana ife kunena kuti, “Ambuye wabwera ndipo akuitana. Chilichonse chomwe Inu mukuchifuna, ndi chanu.”

Lolani mawu amenewo alowe mozama m’mitima mwanu, abale ndi alongo. CHILICHONSE CHIMENE INU MUKUFUNA, AMBUYE WABWERA NDIPO APEREKA ICHO KWA INU.

Atate Akumwamba, O Ambuye, mulole izo zichitikenso. Zinthu zonse izi zimene ine ndanena, “Yesu wabwera ndipo akukuitanani inu.” Kodi Iye akuchita chiyani pamene Iye wabwera? Iye akuitana. Ndipo mulole izo zichitikenso, Ambuye. Mulole Mzimu Woyera Wanu ubwere pakati pa anthu usikuuno, Ambuye Yesu mu mmaonekedwe a—a Mzimu. Mulole Iye abwere usikuuno ndipo adzadziulule Yekha, ndipo potero adzadziwonetsere Yekha.

M’bale Joseph Branham

Uthenga: Kenako Yesu Adabwera Ndipo Adayitana
Nthawi:12:00 PM nthawi ya ku Jeffersonville
Malemba: Yohane Woyera 11:18-28

25-1130 Mbambande

Uthenga: 64-0705 Mbambande

PDF

BranhamTabernacle.org

Yokondedwa Mbambande ya Mulungu,

Moyo wonse weniweni womwe unali mu phesi, ngayaye, ndi mankhusu, tsopano ukusonkhana mwa ife, Mbewu Yachifumu ya Mulungu, Mbambande Zake , ndipo zikupangidwa kukonzekeretsedwa kuuka kwa akufa, kukonzekera kukolola. Alefa wakhala Omega. Woyamba wakhala womaliza, ndipo wotsiriza tsopano ndiye woyamba. Tadutsa mopangidwira ndipo takhala Mbambande za Iye, chidutswa chodulidwa kuchokera kwa Iye.

Mkwatibwi ndi Mkwati ndi Amodzi!

Mulungu adawonetsa mneneri Wake chithunzithunzi cha aliyense wa ife, Mphambande za Iye, mu masomphenya. Pamene Iye adayima pamenepo ndi Ambuye akuyang’ana Mkwatibwi akudutsa pa maso pa Iye,

Iye adationa aliyese wa Ife. Ife tonse maso anthu anali akuyanganira KWAMBIRI PA IYE. Iye anati ife tinali anthu amawonekedwe wokoma kwambiri omwe anali adawawonapo kale m’moyo wake. Panali mpweya chabe mozungulira ife. Ife tinkawoneka okongola kwambiri kwa iye.

Kumbukirani, awa anali MASO MPHENYA a Mkwatibwi; Momwe Iye angadzawonekere, ndipo akutiuza ndendende zomwe Iye anali kuchita. Mvetserani mwatcheru.

Iye adzabwera kuchokera ku mafuko onse, iwo adzapanga Mkwatibwi. Aliyense anali ndi tsitsi lalitali, ndipo analibe zopakapaka, ndipo asungwana okongola kwenikweni. Ndipo iwo anali kundiyang’anitsitsa ine. Icho chinayimira Mkwatibwi kuchokera ku mafuko onse. Mukuona? Iye, aliyense kuyimira fuko, pamene iwo akuguba mwangwiro mu mzere ndi Mawu.

Mkwatibwi, ndiloleni ndinenenso icho kachiwiri kuti, MKWATIBWI, wochokera ku mitundu yonse anali maso awo akuyang’ana pa m’busa wawo, gulu la amuna….AYI, izo si zimene iye ananena. Iwo maso awo Anayang’ana PA MNENERI, kumuyang’anitsitsa iye.

Bola ngati Iwo anali akuyang’ana pa mneneriyo, Iwo anali kuguba mwangwiro. Koma kenako Iye anatichenjeza ife, chinachake chinachitika. Ena anachotsa maso awo pa iye ndikuyamba kuyang’ana china chake chomwe chinangopita mu chisokonezo.

Ndipo, kenako, ine ndinayenera kumuyang’anitsitsa Iye. Iye adzachoka pa malo a Mawu ngati ine sindimuyang’ana iye, pamene iye akudutsa, ngati iye ati apyolepo. Mwina idzakhala nthawi yanga, pamene ine ndatha, mukuona, pamene ine ndatsiriza, kapena chirichonse chimene chiri.

Iye ayenera kumuyang’anira iye, kapena adzachoka pa malo pamene Iye akudutsa. Koma kenako iye akunena kuti mwina ikhoza kukhala nthawi yanga, ndikamaliza, pamene ine sindili pano, Angachoke pamalo posayang’ana maso awo pa iye.

Iye anali kuchenjeza MKWATIBWI momveka bwino, Inu muyenera kuyang’ana maso anu pa Liwu la Mulungu pa matepi. Imeneyo ndiyo njira yoperekedwa ndi Mulungu lero. Limelo ndilo Liwu lomwe lidzalumikizitsa ndi kupangitsa Mkwatibwi kukhala wangwiro. Ngati Inu mutachotsa maso anu ndi makutu anu pa Liwu, Inu mudzachoka mzere ndi kulowa mu chisokonezo.

Uthenga uliwonse umakhala womveka bwino kwambiri ndipo kwambiri zedi. Ndi Mulungu wamphamvu amene akuvundukulidwa pamaso pathu, akudyetsa Mkwatibwi wake ndi Mana yobisika yomwe ife tingadye kokha basi. Ndi wolemera kwambiri kwa ena onse, koma ndi Chakudya Chobisika kwa Mkwatibwi.

Ndi Chiyamiko chotani chomwe Mkwatibwi akukhala nacho, kudyerera pa Mawu, kukhala Mbambande ya Mkwatibwi Wake wa Mawu.

Akuyima yekha, monga Mkwati, “wokanidwa ndi anthu, wonyozedwa ndi kukanidwa ndi mipingo.” Mkwatibwi akuyima motero. Ndi chiani icho? Ndiyo Mbambande Yake, onani, ndiwo Mawu amene Iye angakhoze kugwiritsamo ntchito, kupangidwa kuwonekera. Kukana!

Bwerani mudzalumikizane ndi ife Lamlungu nthawi ya 12:00 PM, nthawi ya ku Jeffersonville, pamene Mulungu akulankhula kudzera mwa mngelo wake wamphamvu, ndikutidula ndi kutipukuta ife kuti tikhale Mbambande ya Mulungu.

M’bale Joseph Branham

Uthenga: 64-0705 Mbambande

Malemba oti muwerenge Chiyanjano chisanayambe:

Yesaya 53:1-12
Malaki 3:6
Mateyu Woyera 24:24
Marko Woyera 9:7
Yohane Woyera 12:24 / 14:19

25-1123 Mulungu Wamphamvu Kuvundukulidwa Pamaso Pathu

Uthenga: 64-0629 Mulungu Wamphamvu Kuvundukulidwa Pamaso Pathu

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Branham Tabernacle,

NDI nthawi za ulemerero bwanji zomwe tikukhala nazo. Mawu ndi Mkwatibwi ndi amodzi ndipo ndi ofanana. Tikukhala kuseri kwa chophimba mum’kupezeka Kwa Ulemerero wa Shekinah. Ife tikuwona Mulungu akudzibisa yekha kuseri kwa khungu mwa m’thenga wake wa mngelo wachisanu ndi chiwiri . Mulungu, kachiwiri, akudzibisa yekha kuseri kwa khungu la munthu mwa aliyense wa ife. Palibe funso lina. Palibe kukayika kwina, Ife NDIFE osankhidwa Ake, okonzedweratu, Mawu opangidwa thupi, Mkwatibwi wangwiro wa Mawu

Pamene Ife tikulumikizana pamodzi kuchokera padziko lonse lapansi, ife tikumvetsera Mawu Ake akulankhula ndi kuwulula kwathunthu Mawu Ake kwa ife Vumbulutso lathunthu kuti Yesu Khristu ali yemweyo dzulo, lero ndi kwa nthawi zonse. Kuwonekera kwa Mawu, Elohim, Mulungu m’thupi akulankhula ndi Mkwatibwi Wake. Mulungu m’thupi alindi moyo ndi kukhala mwa aliyense wa ife. Pulogalamu yomaliza ya Mulungu tsopano ikuwonetseredwa mwathunthu ndikuwonetsedwa mwa aliyense wa ife.

Ife tili okondwa kwambiri komanso othokoza Ambuye kutchedwa achilendo ndi ma nati okhala ndi zolumikizidwako zowoneka mwachilendo. Koma tikudziwa Amene ife tikulumikizidwako naye, ndi omwe tili: Mkwatibwi Wa Mulungu Wolumikizidwa ku Tepi; Ndipo ikutikokera kwa Iyemwini, kukhala yomangililidwako molimba ndi molimba kwambiri pamene ife tikukhala MMODZI NDI IYE, Yesu Khristu yemweyo dzulo, lero, ndi kwa nthawi zonse.

Ife Tatsegula chophimba ndipo talowa mu Lawi la Moto ndipo tikupezamo madalitso a Mulungu! Anthu sangathe kuwona. Sangathe kumvetsa. Koma kwa ife, zili powonekera kwambiri, chifukwa tili mu mzimu womwewo monga Wolemba wathu ndi Mtsogoleri wathu. Ndi Liwu la Mulungu pa Matepi likutsogolera Mkwatibwi Wake.

Tikukhala pa M’kate Wowonetsera, Manna omwe amaperekedwa kwa anthu olekanitsidwa okha. Ndi Chinthu chokhacho chomwe tingadye. Ndi chinthu chokhacho chomwe timaloledwa kudya. Ndipo ndi cha anthu okha omwe aloledwa, okonzedweratu ndipo akudziwa chomwe icho chiri.

Ine ndimangokonda kumumva Iye akutiuza kuti NDIFE NDANI:

Mmodzi yemweyo amene anabwera pansi pa Tsiku la Pentekoste, ndi Mzimu Woyera womwewo umene ukuwonetseredwa lero, kuchokera ku Ulemelero kupita ku Ulemelero, kupita ku Ulemelero. Ndipo wabwerera ku Mbewu Yake yapachiyambi, ndi ubatizo wa Mzimu Woyera; ndi zizindikiro zomwezo, zodabwitsa zomwezo, ubatizo womwewo; mtundu womwewo wa anthu, kumachita mwanjira yomweyo, ndi mphamvu yomweyo, zomverera zomwezo. Izo zikuchokera ku Ulemelero kupita ku Ulemelero.

Ife tabwerera ku Mbewu yopachiyambi ndi ubatizo wa Mzimu Woyera. Zizindikiro zomwezo, zodabwitsa zomwezo, ubatizo womwewo, anthu amtundu womwewo, tikuchita chimodzimodzi, ndi mphamvu yomweyo, kumverera komweko.

IFE NDIFE ANGWIRO, OBWEZERETSEDWA MWATHUNTHU, MKWATIBWI WA MAWU WA TEPI!

Ife tikugonjetsa. Tikukhala. Tikuima. Tikukhala pa Mawu Ake oyera omwe anasungidwira Mkwatibwi Wake. Iye akutipanga ife kukhala angwiro tsiku ndi tsiku. CHIKHULUPIRIRO chathu chafika pamlingo watsopano podziwa kuti NDIFE NDANI, ndipo ndi:

Chosakanidwa, Chosakambirana ndipo koposa zonse, sichili ndi MANGAWA.

Kodi mukufuna kukhala osangalala kuposa momwe mudakhalirapo?
Kodi mukufuna kukhutira 1000% kuti zomwe mukumva ndi pakuti Atero Ambuye? Kodi mukufuna kupangidwa kukhala angwiro ndi Mawu a Mulungu?

Kenako Ine ndikukuitanani kuti mudzalumikizane ndi ife , aku Branham Tabernacle, Lamlungu lino nthawi ya 12:00 PM, nthawi ya ku Jeffersonville, pamene tikumva Mawu a Mulungu akulankhula nafe Mawu a Moyo Wamuyaya: Mulungu Wamphamvu Kuvundukulidwa Pamaso Pathu 64-0629. 

M’bale Joseph Branham

25-1116 Khristu Wozindikiritsidwa Wa Mibadwo Yonse

Uthenga: 64-0617 Khristu Wozindikiritsidwa Wa Mibadwo Yonse

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mawu Amoyo a Mulungu,

Zaka zonsezi ine ndakhala ndikuzibisa izo mu mtima mwanga, kumuphimba Khristu, Lawi la Moto lomwe lija likutanthauzira Mawu, monga zinalonjezedwa.

Ndikudziwa kuti izi zimveka mopanda nzeru kwa anthu ambiri, koma ngati mungopirira ndi mthenga wa mngelo wa Mulungu kwa mphindi zochepa, ndikupempha Mulungu kuti akupatseni vumbulutso lowonjezera, ndikukhulupirira kuti iye, mothandizidwa ndi Mulungu komanso ndi Mawu Ake, komanso molingana ndi Mawu Ake, adzamubweretsa Iye pano pamaso panu. Mulungu, akuulula ndi kudziwonetsera Yekha, kutanthauzira ndi kuulula Mawu Ake.

Ndi chitsitsimutso chotani chomwe chakhala chikuchitika mwezi watha uno mkati mwa Mkwatibwi wa Yesu Khristu. Mulungu, akuulula Yekha kuposa kale lonse, akulankhula ndi Wokondedwa Wake, kupanga chikondi ndi Iye, kumutsimikizira, Ndife Amodzi ndi Iye.

Palibe kukayikira, palibe kusatsimikizika, palibe kukayikira, ngakhale mthunzi wa kukayikira; Mulungu watiululila kwa ife: Liwu la Mulungu likulankhula pa matepi ndi NJIRA YOPEREKEDWA NDIPOSO NJIRA YANGWIRO KWA MKWATIBWI WAKE LERO.

Anapereka njira iyi kuti tisadzafunikire iyo kuisefa, kuifotokoza, kapena kuigwiritsa ntchito mwa umunthu mwanjira iliyonse; zingomverani kokha basi Liwu Loyera la Mulungu likulankhula kuchokera ku mulomo kupita ku khutu kwa aliyense wa ife.

Iye adadziwa kuti tsiku lino likubwera. Iye adadziwa kuti Mkwatibwi Wake angadzadye Manna Obisika okha, Chakudya Chake cha Nkhosa. Sitikufuna kumva china chilichonse kupatula Mawu a Mulungu ochokera kwa Mulungu Mwiniwake.

Ife tadutsa chophimba chimenecho kulowa mu Ulemerero wa Shekinah. Dziko lapansi silingathe kuwona. Mneneri wathu sangatchule mawu ake moyenera. Sangavale bwino. Sangavale zovala za ubusa. Koma kuseri kwa chikopa cha munthu, mkati mwake muli Ulemerero wa Shekinah. Mkati mwake muli mphamvu. Mkati mwake muli Mawu. Mkati mwake muli Mkate Wowonetsera. Mkati mwake muli Ulemerero wa Shekinah, womwe ndi Kuwala komwe kumakhwimitsa Mkwatibwi.

Ndipo kufikira inu mutabwera kuseri kwa chikopa cha katumbu chimenecho, kufikira inu mutatuluka mu chikopa chanu chakale, maganizo anu akale, tizikhulupiriro tanu takale, ndi kubwera mu Kukhalapo kwa Mulungu; pamenepo Mawu amadzakhala chenicheni chamoyo kwa inu, pamenepo inu mumadzutsidwira ku Ulemelero wa Shekinah, zikatero Baibulo limadzakhala Bukhu latsopano, pamenepo Yesu Khristu amakhala yemweyo dzulo, lero, ndi kwanthawizonse. Inu mukukhala mu Kukhalapo Kwake, mukudya mkate wopanda chotupitsa umene wangoperekedwa tsiku limenelo kwa okhulupirira, ansembe okha. “Ndipo ife tiri ansembe, unsembe wachifumu, fuko loyera, anthu achilendo, akupereka nsembe zauzimu kwa Mulungu.” Koma inu mukuyenera kulowa mkati, kuseri kwa chophimba, kuti mukamuwone Mulungu wovundukulidwa. Ndipo Mulungu wavundukulidwa, ndiwo Mawu Ake akuwonetseredwa.

Ndife anthu osamvetseka ku dziko lapansi, koma ife ndi ukhutitsidwa kudziwa kuti Bauti wathu ndi ndani ndiposo onyadira kukhala nati ya matepi Ake, olumikizidwa ku Mawu Ake, chifukwa amatikokera kwa Iye.

Ngati simulumikizidwa ku matepi, siyinu chinthu china koma mulu wa chiphakasa!!!

Tsopano, zindikirani tsopano, Mulungu! Yesu ananena kuti, “Iwo amene Mawu amabwerako, ankatchedwa ‘milungu,’” amenewo anali aneneri. Tsopano, osati munthuyo iyemwini anali Mulungu, osatinso kuti thupi la Yesu Khristu linali Mulungu. Iye anali munthu, ndipo Mulungu amaphimbidwa kuseri kwa Iye.

Mulungu, tsiku lina adaphimbidwa kuseri kwa chikopa cha katumbu. Mulungu, tsiku lina ataphimbidwa ndi thupi la munthu wotchedwa Melkizedeki. Mulungu, adaphimbidwa ndi thupi la munthu wotchedwa Yesu. Mulungu, adaphimbidwa ndi thupi la munthu wotchedwa William Marrion Branham. Mulungu, adaphimbidwa ndi thupi la munthu wotchedwa MKWATIBWI WAKE.

Izo kotero ndikofunikira kukumbukira, koma ambiri akulephera ndipo iwo akuyang’ana china chake basi. Chinthu chomaliza chimene Abrahamu anaona, chinthu chomaliza kuchitika moto usanagwe ndi kuweruza dziko la Amitundu, mwana wolonjezedwa asanabwere, chinthu chomaliza chimene mpingo wachikhristu udzawona mpaka kuwonekera kwa Yesu Khristu ndi Melkizedeki, Mulungu woonekera mu m’thupi, akuulula Mawu Ake kwa Mkwatibwi Wake.

Palibe china chilichonse chomwe chikubwera. Palibe china chilichonse chomwe chinalonjezedwa m’Mawu Ake. Palibe munthu, kapena gulu la anthu lomwe lidzabwere kudzamupanga wangwiro Mkwatibwi.

Ayi! Iwo akufuna kuti azibwera kuno ku mpingo kuti akhale angwiro. Mukuona? Kuti i—ife timapeza chiyanjano wina ndi mzake kuno ku mpingo, koma ungwiro umabwera mwa pakati pa ife ndi Mulungu. Magazi a Khristu ndi amene amatipanga ife angwiro mwa Mzimu Woyera.

Uthenga uwu, Liwu ili, Mawu otsimikiziridwa a Mulungu, akumupanga kukhala wangwiro Mkwatibwi wa Yesu Khristu.

Ndikukupemphani aliyense wa inu kuti abwere kudzamvetsera nafe Liwu la Mulungu pamene likumupanga kukhala wangwiro Mkwatibwi Wake Lamlungu lino nthawi ya 12:00 PM, nthawi ya ku Jeffersonville, pamene tikumva: 64-0617 “Khristu Wozindikiritsidwa Wa Mibadwo Yonse”.

M’bale Joseph Branham

Malemba oti muwerenge Uthenga usanaperekedwe:

Deuteronomo 18:15
Zakariya 14:6
Malaki 3: 1-6
Luka Woyera 17: 28-30
Yohane Woyera 1: 1 / 4: 1-30 / 8: 57-58 / 10: 32-39
Ahebri 1: 1 / 4: 12 / 13: 8
Chivumbulutso 22: 19

25-1109 Chosamvetseka

Uthenga: 64-0614E Chosamvetseka

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mulungu Wokhala Ndi Chikopa Pa Iye.

Ife Sitili kuseri kwa chophimba tsopano, ana aang’ono, Mulungu wabwera powonekera bwino kwa ife. Mulungu wamphamvu wa Kumwamba ndi dziko lapansi, Amene nthawi zonse wakhala akudziphimba kwa anthu monga Lawi la Moto lomwe linachokera kwa Mulungu ndikukhala m’thupi la padziko lapansi lotchedwa Yesu; kenako anabwerera ku Lawi la Moto ndipo anaonekera kwa Paulo panjira yopita ku Damasiko, tsopano wabweranso powonekera bwino ndipo anakhalanso m’thupi la munthu mwa mngelo wake Mtumiki, William Marrion Branham, akuitana Mkwatibwi Wake kwa Iyemwini.

Mulungu anaika mngelo Wake padziko lapansi kuti adziimire ngati kazembe Wake woyikidwa kuti alowe mu zinthu zazikulu zosadziwika zauzimu. Amazindikira ndi kutulutsa zinthu zomwe malingaliro achithupi sangazindikire. Anatumizidwa kuti abweretse chinsinsi cha Mulungu ndi kulosera zinthu zomwe zilipo, ndi zomwe zakhalapo, ndi zomwe zidzakhalapo. Iye ndi Liwu la Mulungu kwa Mkwatibwi.

Ndi chiyani chimenecho? Mulungu, Mulungu kuseri kwa zikopa, chikopa cha munthu. Kulondola kwenikweni.

Otsutsa ambiri masiku ano sangatimvetse ife okhulupirira enieni. Kwa iwo, takhala ngati nati. Amati ndife okhulupirira milungu ndipo timalambira mneneri…

Wotsutsa, masiku pang’ono apitawo, ananena kwa ine, uko mu Tucson. Iye anati, “Inu mukudziwa, anthu ena amakupangani inu kukhala nati, ndipo ena amakupangani inu kukhala mulungu.”

Ine ndinati, “Chabwino, zimenezo zimayenda bwino.” Ine ndinadziwa kuti iye amayesera kuti anditsutse ine. Mukuona?
Iye anati, “Anthu amaganiza kuti inu ndi mulungu.”

Monga momwe zinalili pamene Yesu anali padziko lapansi, ndi chimodzimodzi lero ndi mneneri Wake. Anthu sali kuseri kwa chophimba; achita khungu ku choonadi. Sitikufuna china chilichonse koma njira yoperekedwa ndi Mulungu lero: Iye mwini wophimbidwa mu thupi, Mawu a Mulungu omwe adalembedwa ndikusungidwa kwa Mkwatibwi.

Pamene Mulungu adawonekera padziko lapansi, Iye anali kubisala kuseri kwa chophimba; kuseri kwa khungu la Munthu wotchedwa Yesu. Anaphimbidwa ndikubisala kuseri kwa khungu la munthu wotchedwa Mose, ndipo iwo anali milungu, osati Milungu; koma iwo anali Mulungu, Mulungu mmodzi, akungosintha chigoba Chake, akuchita zomwezo nthawi iliyonse, kubweretsa Mawu awa. Mulungu adapanga mwanjira imeneyo.

Tangolumikizidwa ku Mawu, Uthenga wa nthawi ino. Tsopano watipanga Mawu ophimbidwa kuseri kwa thupi la munthu. Mkwatibwi ndi Mkwati ndi amodzi. Mulungu ndi mmodzi, ndipo Mawu ndi Mulungu! Talumikizidwa ndi Mawu.

Mwachisoni, kusiyana pakati pa okhulupirira lero ndikuti amamva kuti timayika kwambiri pa mneneri wotsimikiziridwa wa Mulungu. M’malo mwake, akufuna kuyika utsogoleri umenewo kwa abusa awo.

Mulungu sasintha pulogalamu Yake; amatumiza MUNTHU MMODZI kuti atsogolere Mkwatibwi Wake. Ndi Mzimu Wake Woyera mwa aliyense wa ife, kutitsogolera ndi LAWI LA MOTO.

Mawu amadza kwa mmodzi. Mu m’badwo uliwonse, chimodzimodzi, ngakhale mu mibadwo ya mpingo, kuyambira kwa woyamba womwe mpaka kwa wotsiriza. Enawo ali ndi malo awo awo, izo nzoona, zindikirani, koma muzikhala kutali ndi Lawi la Moto ilo. Mukuona?

KOMA TIKUMVA CHIYANI LERO…CHINTHU CHOMWECHO.

Inu mukukumbukira zimene Datani ndi iwo ananena uko? Iwo anati, “Tsopano, Mose, dikira apa miniti chabe! Iwe ukudzitengera wekha kwambiri, mwaona. Tsopano, aliponso anthu ena pano omwe Mulungu wawaitana.”

Sitikutsutsana ndi utumiki; Mulungu wawaitana, koma abale ndi alongo, ngati m’busa wanu sakuika Mawu a Mulungu ngati Mawu ofunikira kwambiri omwe muyenera kumva posewera matepi mu mpingo wanu, sakukutsogolerani ku njira yoperekedwa ndi Mulungu.

Izo ndi zoona. Iwo, mmodzi aliyense, amatsatira mwabwino nthawizonse pamene iwo anali kutsatira, koma pamene wina anayesera kuti adzikweze ndi kutenga malo a Mulungu amene Iye anamupatsa Mose, yemwe anali wokonzedweratu ndi wodzozedweratu ku ntchito imeneyo, kuyesera kuti aitenge iyo, moto unatsika pansi ndipo unadzatsegula nthaka ndi kuwamezera iwo mmenemo. Mukuona? Mukuona? Muzisamala. Mukuona?

Tonsefe tiyenera kulumikizidwa ku Mawu amene analankhulidwa ndi kuikidwa pa matepi. Umenewo ndiye Mtheradi wa Mulungu. Ndiwo Mawu okhawo omwe Mkwatibwi angagwirizane nawo. Utumiki sudzagwirizanitsa Mkwatibwi, koma Mawu a Mulungu okha pa matepi.

Ine sindingachite kalikonse popanda inu; inu simungachite kalikonse popanda ine; komanso sitingachite kalikonse popanda Mulungu. Kotero, pamodzi timapanga thunthu, chilumikizocho. Mulungu ananditumiza ine pa cholinga; inu mukakhulupirira izo, ndipo apo izo zizichitika. Basi ndi zimenezo, Mwaona, kutsimikiziridwa mwangwiro.

Pokhapokha pamodzi zimapanga CHIMODZI, kulumikizana. Mulungu anatumiza William Marrion Branham pa cholinga chimenecho. Ndiye, Pokhapokha ngati mukhulupirira, kodi chidzachitika; zatsimikiziridwa bwino.

Sindine amene ndikunena zimenezo, abale ndi alongo. NDI MULUNGU AKUNENA ZIMENEZO KUDZELA MWA MNENERI WAKE. Musalole munthu aliyense kukuuzani zosiyana kapena kuyesa kukufotokozerani mosiyana. LIWU LA MULUNGU LOKHA PA MATEPI NDILOMWE LINGAGWIRIZANITSE NDI KUMUFIKITSA MKWATIBWI KU UNGWIRO. NDI NJIRA INA ILIYONSE, INU SIMUDZAKHALA MKWATIBWI.

Kotero ine ndikuganiza kuti akuluakulu onse a ife timaganiza chinthu chomwe chomwecho. Mulungu, wokhala ndi khungu pa Iye! [Malo osajambulidwa pa tepi—Mkonzi.] Mulungu, wokhala ndi khungu pa Iye! Izo zikhoza kumveka ngati nati, kwa dziko, koma iyo ikukokera anthu onse kwa Iye.

Kodi mwamva zomwe wangonena kumene? Mulungu wokhala ndi khungu akukoka anthu onse kwa Iye.

Pamene dziko lapansi likulumikizidwa ndi nati, ife tikulumikizidwa ndi Liwu la Mulungu ndipo timatchedwa Mkwatibwi. Likutikoka kuti tituluke mu chisokonezochi, kupita ku Kukhalapo kwa Mulungu. Ife ndife nati ya Mawu a Mulungu.

Bwerani mudzalumikizidwe ndi Mawu a Mulungu limodzi nafe Lamlungu lino nthawi ya 12:00 P.M., nthawi ya ku Jeffersonville, pamene ilo likukokela anthu onse kwa Iye.

M’bale Joseph Branham

Uthenga: chosamvetseka. 64-0614E

Malemba: 1 Akorinto 1:18-25. / 2 Akorinto 12:11

25-1102 Kuvundukulidwa Kwa Mulungu

Uthenga: 64-0614M Kuvundukulidwa Kwa Mulungu

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mawu Opangidwa Kuwonetseredwa,

Kodi tingaganizire za Iwo! Lawi la Moto lomwelo lomwe linabwera pa anthu omwe analemba Baibulo ndi Lawi la Moto lomwelo lomwe tikulimva tsiku lililonse, kutanthauzira zinsinsi zonse za Baibulo kwa ife: Mawu a Mulungu Opangidwa kuwonetseredwa!

Mulungu anadziphimba Yekha mwa aneneri Ake akale kuti alankhule Mawu Ake kwa iwo. Ndicho chimene Iye anachita panthawiyo. Koma mumtsiku lathu lino, mneneri wathu, William Marrion Branham anali Mawu amoyo kwa anthu, ophimbidwa ndi Lawi la Moto.

Kudzozako ndi munthu. Mawu akuti Khristu amatanthauza wodzozedwayo, mwaona, “wodzozedwayo.” Ndiye, Mose anali Khristu mu masiku ake, iye anali wodzozedwayo. Yeremiya anali Khristu mu masiku ake, ali ndi gawo la Mawu a tsiku limenelo.

Mulungu amatanthauzira Mawu Ake Omwe. M’bale Branham anawalankhula; Mulungu anawamasulira. Iye anali ndi Mawu. Osati gulu, William Marrion Branham! Mulungu anapeza MUNTHU MMODZI. Sangathe kupeza malingaliro awiri kapena atatu osiyana ndi malingaliro osiyana. Iye akutenga MUNTHU MMODZI, ndipo anakhala Mawu amoyo a Mulungu ophimbidwa kuseri kwa thupi la munthu.

Sitili kuseri kwa chophimba chimenecho, ana aang’ono. Mulungu waonekera bwino kwa inu. Chophimba chakale chachipembedzo ndi chachikhalidwe chang’ambidwa ku Mawu a Mulungu, kuti chiwonekere! Mu tsiku lomaliza lino, chophimba chachikhalidwecho chang’ambidwa, ndipo apa pali Lawi la Moto. Apa Iye ali, akuwonetsa Mawu a tsiku lino. Chophimbacho chang’ambika.

Mudzawawone matepi amenewo pamene iwo azibwera, mudzaiwone imodzi iliyonse, momwe Iwo akubwerera momveka ndi momveka; ngati inu muli ndi makutu omvera, mwaona, maso openyera.

Ndicho chimene chikuchititsabe khungu anthu lero. Amafuna kunena kuti amakhulupirira kuti mneneri wa Mulungu ndiye anabweretsa Mawu, koma tsopano kudzoza kumeneko kuli pa ena kuti atitsogolere, osati mneneri.

Mneneri anatiuza kuti Mulungu sangaswe Mawu Ake. M’masiku otsiriza, ziyenera kukhala chimodzimodzi kachiwiri. Mulungu sangasinthe njira Yake, kapena kusintha Mawu Ake. Iye anati Sanasinthe. Iye nthawi zonse wakhala akutumiza aneneri Ake osati kuti abweretse Mawu Ake okha, komanso kuti atsogolere Mkwatibwi Wake.

Monga izo zimachitikira mu m’badwo uliwonse, Umulungu kuphimbidwa mu mnofu wa munthu. Zindikirani, Iye anatero. Aneneri anali Umulungu, utaphimbidwa. Iwo amakhala Mawu a Mulungu (ndi kulondola uko?) ataphimbidwa mu mnofu wa munthu. Kotero, iwo sanamuzindikire Mose wathu chonchobe, mwaona, Yesu.

Tsopano si Mawu olembedwa kwa ife okha, ndi zenizeni. Tili mwa Iye. Tsopano tikusangalala. Tsopano tikumuona Iye. Tsopano tikumuona Iye, Mawu, akudziwonetsera Yekha.

Kenako, timakhala gawo la Iye. Ndife chophimba chomwe chimamuphimba Iye. Ndife gawo la Iye; bola Khristu ali mwa inu, monga Khristu anali wa Mulungu.

Tikumanga kachisi wa Khristu kuseri kwa chophimba cha khungu lathu la munthu. Ndife makalata olembedwa, Mawu olembedwa. Ndife Mawu omwe alembedwa, owonetsedwa.

Ndipo pamene inu muwawona Mawu akuwonetseredwa, inu mwawawona Atate, Mulungu, chifukwa Mawu ndi Atate. Mawu ndi Mulungu. Ndipo Mawu, akamawonetseredwa, ndi Mulungu Mwiniwake akutenga Mawu Ake Omwe ndi kumawawonetsera Iwo pakati pa okhulupirira. Palibe kanthu kamene kangawapange Iwo kukhala amoyo koma okhulupirira, okhulupirira basi.

Mulungu, wophimbidwa mu thupi la munthu, akulankhula ndi kuwulula Mawu Ake kwa ife tsiku ndi tsiku. Mulungu mu thupi la munthu akukhala mwa aliyense wa ife.

M’bale Joseph Branham

Uthenga: 64-0614M – “Kuvundukulidwa Kwa Mulungu “
Nthawi: 12:00 P.M. Nthawi ya ku Jeffersonville

Kumbukirani kusunga nthawi ya masana

25-1026 Yang’anani Kutali Kwa Yesu

Uthenga: 63-1229E Yang’anani Kutali Kwa Yesu

PDF

BranhamTabernacle.org

Okondedwa Iwo Omvera Matepi,

Nthawi yafika yoti aliyense adzifunse kuti: “Ndikamamvetsera matepi, ndi Liwu lotani limene ndimamva? Kodi basi ndi Liwu la William Marrion Branham, kapena ndimamva Liwu la Mulungu la tsiku lathu? Kodi ndi liwu la munthu, kapena ndikumva Pakuti Atero Ambuye ? Kodi ndikufunika wina womasulira zomwe ndikumva, kapena kodi Mawu a Mulungu safunikira kutanthauzira?”

Yankho lathu ndi ili: Ife tikumva Mawu Olankhulidwa osandulika thupi. Tikumva Alefa ndi Omega. Tikumva Iye, Lawi la Moto, akulankhula kudzera m’milomo ya munthu monga momwe Iye ananenera kuti adzachitira m’masiku athu.

Sitimva munthu, timamva Mulungu, yemweyo dzulo, lero, ndi kwa nthawi zonse. Mawu a Mulungu omwe ndi achangu, amphamvu kuposa lupanga lakuthwa konsekonse, odula ngakhale fupa, ndi ozindikira malingaliro omwe ali mumtima.

Izo zavumbulutsidwa kwa ife kuti chimene Iye anali pamene ankayenda mu Galileya ndi chomwechi chimene Iye ali usikuuno ku Jeffersonville; chinthu chomwecho chimene Iye ali ku Branham Tabernacle. Ndi Mawu a Mulungu akuonekera. Chimene Iye anali panthawiyo, Iye ali usikuuno, ndipo adzakhalapo kwa nthawi zonse. Chimene Iye anati adzachita, Iye wachita.

Munthuyo si Mulungu, koma Mulungu akadali ndi moyo ndipo akulankhula ndi Mkwatibwi Wake kudzera mwa munthuyo. Sitiyenera kulambira munthuyo, koma kulambira Mulungu mwa munthuyo; pakuti iye ndi munthu amene Mulungu anasankha Iye kukhala LIWU LAKE ndikutsogolera Mkwatibwi Wake m’masiku otsiriza ano.

Chifukwa Iye watipatsa bvumbulutso lalikulu la nthawi yotsiriza, tsopano tikhoza kuzindikira YEMWE IFE TILI, Mawu osandulika kukhala thupi m’masiku athu ano. Satana sangatinyengenso, chifukwa ife tikudziwa kuti ndife namwali wake obwezeretsedwa mwathunthu, Mkwatibwi wa Mawu.

Liwu limenelo linatiuza kuti: Zonse zomwe ife tinkazisowa zapatsidwa kale kwa ife. Palibe chifukwa chodikira. Ilo lalankhulidwa, NDI LATHU, NDI LA IFE. Satana alibe mphamvu pa ife; wagonjetsedwa.

Inde, Satana akhoza kutibweretsera matenda, kuvutika maganizo, ndi chisoni, koma Atate watipatsa kale mphamvu yoti timutulutsire kunja…IFE TIMANGOLANKHULA KOKHA MAWU, Ndipo iye ayenera kutichokera….osati chifukwa chakuti ife tanena choncho, koma chifukwa chakuti MULUNGU ANANENA CHONCHO.

Mulungu yemweyo amene analenga agologolo, pamene panalibe agologolo. Zimenezo zinamupatsa Mlongo Hattie chofuna cha mtima wake: ana ake aamuna awiri. Amene anachiritsa Mlongo Branham chotupa dzanja la dokotala lisanamukhudze. Iye ndi MULUNGU YEMWEYO amene sali ndi ife kokha, KOMASO IYE ALI NDI MOYO NDIPO AKUKHALA MWA IFE. IFE NDIFE MAWU OSANDULIKA KUKHALA THUPI.

Tikamaona ndi kumvetsera Mawu pa matepi, timaona ndi kumva Mulungu akudziulula Yekha mu thupi la munthu. Timaona ndi kumva amene Mulungu anatuma kuti atitsogolere ku Dziko Lolonjezedwa. Timadziwa kuti Mkwatibwi yekha ndiye adzakhala ndi bvumbulutso limenero, motero takhala opanda mantha. Palibe chifukwa chokhala ndi manjenje, kuvutika maganizo, kukhumudwa, kudabwa kapena kuda nkhawa…NDIFE MKWATIBWI.

Mvetserani ndi kukhala ndi moyo, m’bale wanga, khalani ndi moyo!
Mvetserani Yesu tsopano ndi kukhala ndi moyo;
Pakuti zajambulidwa pa matepi, aleluya!
Ndi kuti timvetsere ndikukhala ndi moyo.

O, Mkwatibwi wa Yesu Khristu, ndi tsiku lalikulu bwanji lomwe tikukhalamo. Zimene tikuyembekezera, mphindi ndi mphindi. Tsiku lililonse tsopano tidzawona okondedwa athu, ndiye, mu mphindi ya kuthwanima kwa diso, tidzachoka pano ndipo tidzakhala nawo mbali ina. Zili moyandikira kwambiri kotero kuti zikuwoneka kuti tingazikhudze izo…ULEMERERO!

Bwerani Mkwatibwi, tiyeni tisonkhanenso mozungulira Mawu a Mulungu Lamlungu lino nthawi ya 12:00 PM, nthawi ya ku Jeffersonville, pamene Ife tikumumva Iye akulankhula nafe Mawu a Moyo Wamuyaya.

M’bale. Joseph Branham

Uthenga: 63-1229E Yang’anani Kutali Kwa Yesu

Malemba Opatulika:
Numeri 21:5-19
Yesaya 45:22
Zekariya 12:10
Yohane Woyera 14:12