All posts by admin5

26-0208 Mafunso ndi Mayankho #3

Uthenga: 64-0830M Mafunso ndi Mayankho #3

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Wobadwa mwa Khristu,

Kodi wina angayike bwanji mkati mawu a chabe aumunthu chikondi ndi chisangalalo chomwe chili m’mitima mwathu kuti tidziwe Vumbulutso lenileni la Mawu Ake a tsiku lathu? Kuganiza, ife sitinali ndi chochita ndi icho, koma IYE, WAMKULU INE NDILI, mwa kusankha kwa IYE mwini, anatikonzeratu IFE kuti tikhale ndi chinthu chachikulu kwambiri chomwe Iye angatipatse, VUMBULUTSO LA MAWU AKE A TSIKU LATHU.

Iye anadikira, mpaka nthawi yonse itakwana, kuti apume mpweya wa moyo mwa ife, kotero kuti ife timumve Iye akulankhula nafe ndi kunena kuti:

Tsopano, ine ndayesa mwa kupambana kwanga k—k—kuti ndikuuzeni anthu inu ndi kukutsogolerani inu monga bambo angawatsogolere ana ake. Inu ndinu ana anga; ine ndakubalirani inu kwa Khristu kudzera mu Uthenga uwu umene ine ndikuulalikira. Mukuona? Ndipo i—i—ine ndikufuna inu kuti mukule kwathunthu kukhala ana okhwima, k—kapena ana. Ndipo ine ndikufuna kuti ndidzakuperekeni inu kwa Khristu tsiku limenelo, monga Paulo anati, “Namwali wangwiro.” Mulibe chinthu china mu Mawu amenewo koma chimene mtima wanu ungavomereze kuti “ameni” kwa icho.

Mulungu, polankhula kudzera mwa mngelo wake wamphamvu, akutilunjikitsa ndi kutitsogolera ife, Mkwatibwi wa Yesu Khristu. Ife ndife ana ake akucha mokwanira, namwali woyera mtima. Ndipo mwa chisomo Chake chodabwitsa, ife timavomereza Mawu aliwonse omwe ife timamva ndi AMEN! Ndi kutanthauzira kwangwiro kwa Mawu ndi chitsimikizo Chaumulungu!

Ngati Mawu omwe ife tikumva pa matepi ndi: kutanthauzira kwangwiro kwa Mawu, kodi Mkwatibwi wa Yesu Khristu akusowa chiyani china?…PALIBE!

Iye watisankha IFE, gulu lake laling’ono losankhidwa ndi dzanja, kuti tikhale ndi Vumbulutso lenileni la Mawu Ake la tsiku lathu lino. Ife ndi amene omwe Iye adasankha kukhala padziko lapansi, m’matupi a aumunthu, panthawi ya ulamuliro wa zana chikwi a mileniyamu.

Abwezi, tiyeni tikhazikike pa pamenepo mwa kamphindi.

Ife tidzakhala ndi thupi laulemerero padziko lapansi pomwe pano. Ife tidzakhala tikudya, kumwa, kumanga nyumba, kukhala monga momwe tikuchitira tsopano kwa zaka chikwi. Kudzakhala mbindikiro wa ukwati wathu komwe Mkwatibwi (IFE) ndi Mkwati (Ambuye Yesu Khristu) adzakhala MMODZI.

Ife tikuyang’anira ndi kuyembekezera nthawi yaulemerero iyi mphindi iliyonse ya tsiku lililonse. Ili pafupi kwambiri moti zikuoneka kuti tingathe kuikhudza. Ine ndikukhulupirira, ndi mtima wanga wonse, izi ndi zomwe zikuchitika kwa ife lero:

O, chilumikizano chauzimu chija cha Khristu ndi Mpingo Wake tsopano, pamene mnofu ukusandulika Mawu, ndipo Mawu akusandulika mnofu, kuwonetseredwa, kutsimikiziridwa. Basi zomwe Baibulo linati zikanadzachitika mu tsiku lino, izo zikuchitika, tsiku ndi tsiku. Bwanji, izo zikuwunjikana mofulumira kwambiri kunja uko, mu zipululu izo, ndi zinthu zomwe zikuchitika, mokuti ine sindingakhoze ngakhale kuyendera limodzi nazo izo. Ife tayandikira Kudza kwa Yesu, kuti alumikizane ndi Mpingo Wake, komwe Mawu akusandulika Mawu.

Uthenga uliwonse umene ife timamva, ndiye kuti akutipatsa ife Vumbulutso lochuluka. Likuwonjezeka mofulumira kwambiri moti ife sitingathe kulekana nalo. Tikuona Mawu akusandulika Mawu kuposa kale lonse. Palibe mthunzi umodzi wa kukayika kumodzi; mwa Vumbulutso, ife TIMADZIWA bwino lomwe amene Ife tiri.

Iye akulumikiza Mkwatibwi Wake monga momwe Iye ananenera kuti adzachitira, ndipo ife ndi gawo la Icho. Ife tikuchiona icho Chikuchitika ndi maso athu. Ena sangachione kapena kuchimvetsa. Si cha iwo , ICHO NDI CHA IFE, ANA AKE OBADWA.

Mkwatibwi adali ndi mafunso oti afunse mneneri.

Kodi izo ndizokwanira kungomvera Liwu la Mulungu pa matepi okha? Mulungu adayankha ndipo adati: INDE!!

Kodi ana athu angapezenso zonse zomwe iwo akufuna kuti akhale Mkwatibwi wa Khristu pongomvera matepi: INDE!!

Kotero, Zonse zomwe Mkwatibwi amafuna zili PA MATEPI.

Ife tikudziwanso kuti Mulungu wapereka njira zina zambiri kwa ana Ake.

“Ndi mikwingwirima Yake inu munachiritsidwa.” Tsopano, choyamba Mawu amanena choncho, zimenezo ziyenera kukhala zokwanira, koma ngati simukukhulupirira mu Mawu, ndiye kuti pali mphatso mu Mpingo, monga amuna omwe ali ndi mzimu wodziwa momwe angaphunzitsire zimenezo, zomwe zidzapangitsa kuti izo zikhale zomveka kwa inu, ndiko kuti, ndi chikhulupiriro kukhulupirira.

Ife tikuthokoza kwambiri Mulungu wapereka amuna omwe ali odzonzedwa wodziwa momwe angaphunzitsire machiritso ndi Mawu Ake kuti awamveketse bwino kwa ena, koma Mkwatibwi Wake akufuna NJIRA YAKE YANGWIRO YOPEREKEDWA. Ndicho chokhacho chomwe IFE TIKUFUNA.

Ndikufuna kukuitanani kuti mubwere kulumikizana ndi Branham Tabernacle Lamlungu lino nthawi ya 12:00 PM, nthawi ya ku Jeffersonville, pamene tikumva: Mafunso ndi Mayankho #3 64-0830M.

Ndizosangalatsa bwanji kukhala ndi Vumbulutso la Mawu Ake ndikudziwa kuti ndife Mawu opangidwa thupi.

M’bale Joseph Branham

26-0201 Mafunso ndi Mayankho #2

Uthenga: 64-0823E Mafunso ndi Mayankho #2

PDF

BranhamTabernacle.org

Okondedwa Ana A Mphungu,

Kumene kuli nyama, ndi komwe Mkwatibwi adzasonkhana pamodzi. Ndipo kwa ife, pali malo amodzi okha angwiro omwe ife tingapezeko Manna ya tsopano amenewo: mwa kukanikiza kusewera ndikumva Liwu la Mulungu pa matepi.

Kakamba za Manna YATSOPANO, kodi tingayambe kuganiza zomwe tili nazo ku songa ya Chala chathu? Liwu lenieni la Mulungu likulankhula ndi Mkwatibwi Wake wokondedwa pa tepi, komwe kulibe kuganiza, kulibe kudabwa, kulibe kufunsa kapena kukayikira kuti yemwe tikumva ndi Mulungu, pogwiritsa ntchito liwu la munthu, kulankhula Pakuti Atero Ambuye kwa Mkwatibwi Wake.

Mwa vumbulutso, ife timakhulupirira kuti Ndi malo OKHAWO omwe ife tingapiteko ndi kupumulitsa miyoyo yathu kuti Mawu omwe tikumva si mawu a munthu, komanso sikutanthauzira kwake kapena lingaliro lake kapena wonjezeredwa kwa Iwo, koma iwo Ndi Mawu oyera a Mulungu akulankhula kwa ife ana a Mphungu, akuwulula Mawu Ake.

Ife timasonkhana mozungulira Mawu. Timawerenga Mawu Ake m’Mabaibulo athu. Ife iimamvanso anthu odzonzedwa ndi Mulungu ndinso amuna oyitanidwa odzazidwa ndi Mzimu Wake Woyera, akubwereza ndi kulalikira Mawu a Mulungu, koma mutsiku lathu , Mulungu wapereka malo momwe ife tingamve MAWU Ake ANGWIRO AKULANKHULIDWA, mwa kukanikiza kusewera.

Atate Koteronso amapatsanso Mkwatibwi Wake mwayi wofunsa mafunso omwe anali pamtima pathu kuti tikhale ndi yankho langwiro:

  • Kodi Satana angagwiritse ntchito mphatso ya malilime kapena ulosi mwa munthu amene ali ndi Mzimu Woyera?
  • Kodi Yesu ankatanthauza chiyani mu Mateyu 12, vesi 32?
  • Chonde fotokozani 1 Akorinto 13:8-12.
  • Kodi akazi ndiwololedwa kugwira ntchito mmabwalo awunyinji wa anthu pomwe iwo alinaye mwamuna ndi ana athanzi labwinobwino?
  • Kodi n’kulakwa kuti mkazi azimanga tsitsi lake?

Mulungu wapereka njira zambiri zodalitsira ndi kulimbikitsira Mkwatibwi Wake, koma pali malo amodzi okhawo omwe wapereka komwe Mkwatibwi Wake angakhale ndi chidaliro chama peresenti 100 kuti chomwe iwo akumva ndi MAWU AKE ANGWIRO. Kasupe Mmodzi wa Madzi Amoyo komwe Ana Amphungu amatha kumwa kuchokera ku iye komwe kulibe kuthekera kwa kuipitsidwa kulikonse. KUKANIKIZA KUSEWERA.

Ine ndikukuitanani inu kuti mudzamwe kuchokera ku Kasupe ameneyo Lamlungu lino nthawi ya 12:00 PM, nthawi ya ku Jeffersonville, komwe ife tidzava 64-0823E “Mafunso ndi Mayankho #2.”

M’bale Joseph Branham

26-0125 Mafunso ndi Mayankho #1

Uthenga: 64-0823M Mafunso ndi Mayankho #1

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Branham Tabernacle,

Moni kwa Mkwatibwi wa Yesu Khristu kuchokera kuzungulira padziko lonse lapansi, omwe amakhulupirira kuti Branham Tabernacle, Liwu la Mulungu, ndi tchalitchi chawo cha kwawo komwe iwo akudyetsedwa mwauzimu ndi Mana obisika omwe asungidwa ndi kusungidwira Mkwatibwi wa Khristu.

Kuno ndi kwathu kokhazikika; kuno ndi likulu langa; kuno ndi kumene ife tinakhazikikako. Tsopano, sungani zimenezo mmalingaliro ziribe kanthu chomwe chingachitike. Tsopano, ngati ndinu anzeru, mugwira chinachake. Ziribe kanthu chomwe chingachitike, lino ndi likulu lathu, pomwe pano!

Okhulupirira ambiri nthawi zonse akhala osamvetsetsa kapena kuyika lingaliro lawo kapena kutanthauzira kwawo ku zomwe mneneri ananena apa, koma akuuza Mkwatibwi molunjika, “ngati Inu muli anzeru, mugwira china chake, ili ndiye likulu lathu, komwe kuno!

Kodi Iye ankatanthauza chiyani pa zimenezo?

pomwe m’bale Branham anali pano, ambiri sanamumvetse bwino Iye ndipo ankaganiza kuti Mkwatibwi ayenera kupita ku Arizona ndi kumutsatira iye kumeneko, kuti adzapite mu Mkwatulo. M’bale Branham anawayankha momveka bwino kuti: KHALANI PANO, AWA NDIWO MALO.

gulu lalikulu lonse la iwo linanyamuka kupita njira imeneyo, ndipo iwo ankafuna kuti apite uku ndi kukachita izo, ine nditatha kuwauza iwo kuti akhale pamenepo. Mukhale pamenepo, mukhale pomwe pano; awa ndiwo malowo.

Anthu ananyamuka kuchokera kulikonse mu United States kupita ku Arizona, koma iye anawauza momveka bwino kuti: Khalani pomwe pano, awa ndiwo malowo!

Khalani ku Jeffersonville? Ndicho chimene ananena!

Vumbulutso langa ndi lakuti, anali Mulungu, akulankhula kudzera mwa mneneri wake ndikuuza anthu kuti, “KHALANI NDI MATEPI.” Awo NDIWO MALOWO!

Iye kotero anakwiya ndipo iye anati ankayenera kuchitapo chinachake ndi anthu onsewo.Kodi iye ayenera kuti anachita chiyani? Kodi ndi ku tchalitchi chiti komwe Iye akanawatumizako iwo? Kodi iwo ankayenera kupita kuti? Kodi M’bale Branham anati iye ayenera kuti anachita chiyani?

Kotero tsopano, ine ndikuyenera ndiwabweretse ana amenewo kuno kuti adzapeze chinachake choti adzadye. Iwo ali kumusi uko mchipululu akuvutika ndi njala.

Iye sananene kuti iwo ankafunikira kupita kutchalitchi chapafupi ndikukatengako tizidutswa tating’onoting’ono tomwe iwo angadye. Iye anati ankayenera KUWABWERETSELANSO KUNO chinachake choti adzadye, apo kupanda kutero AKANAFA NDI NJALA.

VUMBULUTSO LANGA, ABWENZI.

Tsopano, musatinso kachiwiri musamuvetsenso molakwika, kapena kunena zomwe iye sananene, ponena kuti, “M’bale Branham amafuna kuti wokhulupirira aliyense apite kukakhala ku Jeffersonville kuti akhale Mkwatibwi.” M’bale Branham ankadziwa anthu onsewo, ndipo wokhulupirira ALIYENSE wochokera padziko lonse lapansi, sakanatha kuchoka ndikukhala ku Jeffersonville. Zimenezo sizikanatheka. Ndiye iye ankatanthauza chiyani? Iye Anali KUGWIRIZANITSA Mkwatibwi wa Khristu mozungulira matepi omwe anajambulidwa ndi kusungidwa kuti Mkwatibwi adye.

Uthenga uwu, Liwu ili, ndi Mawu Olankhulidwa ndi Mulungu lero ndipo ilo lidzagwirizanitsa ndi kumupanga Mkwatibwi wa Yesu Khristu kukhala wangwiro.

Nyama ndi chimene mphungu zimadya. Tsopano, mphungu imafanizidwa mu Baibulo, ngati mneneri. Mneneri ndi mphungu. Mulungu—Mulungu amadzitcha Yekha mphungu, ndipo ndife “ana a mphungu” ndiye, o—okhulupirira. Inu mukuona? Ndipo nyama imene izo zimadya ndi chiyani? Ndi Mawu. Kulikonse kumene kuli Mawu, chikhalidwe chenicheni cha mbalame chidzadziwonetsera chokha.

Kodi Mawu a Ambuye oyera ali kuti , otsimikizilidwa, osakhala osamvetsetseka, Pakuti Atero Ambuye wa lero? Pali malo amodzi okha, Matepi.

Ndikhoza kupitiriza, ndi chobwereza pa pachobwereza, koma Uthenga uwu ndi zomwe M’bale Branham ananena zimatenga vumbulutso kuchokera kwa Mulungu. Tiyenera kuwerenga pakati pa mizere ndi vumbulutso, koma muzinena zomwe iye adanena. Pakuti Ndi Mawu OYERA.

Mafunso ndi Mayankho a lero ndi zomwe NDIMAKHULUPIRIRA.

Masiku ano, atumiki ambiri akuuza anthu kuti pokhala ndi Tchalitchi cha Mnyumba cha Tepi ife tasiya Mawu ndi zomwe M’bale Branham anati ife tichite. Amavelera kuti ife tiyenera kupita ku zomwe iwo amazitcha ndikuzitenga ngati tchalitchi.

Zoona Zilipo zambiri ,zobwereza zambiri momwe M’bale Branham akunena momveka bwino izi.

“Tsopano, inu muzipita ku tchalitchi china chabwino cha Uthenga wonse ndipo mukazipezere tchalitchi cha kwanuko.”

Ndipo ine ndimakhulupirira zimenezo ndi mtima wanga wonse, chifukwa iye anatero. Koma ine ndikukhulupirira kuti ife tikuchita zimenezo mwa KUKHALA NDI TCHALITCHI CHA PA NYUMBA CHA TEPI. Malo athu si omwe ali ofunika kwa Ambuye. Imeneyo ndi nyumba chabe. Koma ntchito yathu kwa Ambuye ndikukhalabe ndi Mawu Ake, OSATI MALO KAPENA NYUMBA. Malowo sapulumutsa ndi kupangitsa Mkwatibwi kukhala wangwiro, MAWU AMACHITA.

Ngati ndipita ku nyumba ya tchalitchi, koma ayiwala CHINTHU CHACHIKULU: kumva Liwu la Mulungu mwa kukanikiza Kusewera, ndipo angolowetsapo m’malo mwake pongomva KOKHA atumiki akulalikira Uthenga, kodi zimenezo zidzakukhutiritsani kotheratu ndi kudyetsa moyo wanu wonse? Zingakhutiritse moyo wanu, m’bale wanga ndiso mlongo wanga, koma sizidzakhutiritsa Mkwatibwi.

Ndiloleni ine nditsindike apa ndikunena kuti pali anthu zikwizikwi omwe alibe nyumba ya tchalitchi yoti apiteko. Kodi iwo atayika? Ngati iwo alibe m’busa kapena tchalitchi, kodi zimenezo zikutanthauza kuti iwo sangakhale Mkwatibwi? Ngati inu mukukhala pamtunda wa makilomita 100 kuchokera ku nyumba ya tchalitchi, kodi inu mukuyenera kupita ku tchalitchi chimenecho? Koma ngati ine ndikukhala kutali, ine sindiyenera kutero? Ine Ndiyenera kulumikizidwa ku mlaliki, koma ine sindingathe kulumikizidwa ku matepi? Nyumba yowoneka ndi maso ndi imene mneneri akunena kuti ndi chinthu chofunika kwambiri chomwe ife tiyenera kupitako?

Kodi mneneriyo ankafuna kumubweretsa Mkwatibwi kuti?

Ngati inu simungathe kubwera kuno ku kachisi, kapezeni tchalitchi china kwinakwake; muzikapita kumeneko.

Kamodzinso, kodi chisankho chake choyamba chotumiza anthu chili kuti? Ku Branham Tabernacle, Mawu, matepi. Ndicho chimene Mulungu wapereka Mkwatibwi Wake kuti achite mu nthawi ino yotsiriza, ndipo tikuchita izi tsiku lililonse NDI Lamlungu lililonse.

Kotero ine simukundiva molakwika. INE SINDIKUNENA KUTI muyenera muzilumikizidwa pa intaneti ku matepi ndi Branham Tabernacle kuti mukhale Mkwatibwi. Ine SINDINENA KUTI inu simukuyenera kupita kutchalitchi.Ine SINDIKUNENA KUTI simungamvere atumiki. Ngati inu mukukhulupirira zimenezo, Inu mwachoka pa Mawu. Ine ndikunena kuti kumva Liwu la Mulungu pa matepi ndilo Liwu lofunikira kwambiri lomwe MUYENERA KUMVA, ndipo ndikukhulupirira kuti m’busa aliyense ayenera kusewera Liwu limenelo, matepi, m’matchalitchi awo. Koma iwo apanga zifukwa zonse zomwe zilipo KUTI OSATI ASASEWERE MATEPI. Ngati umenewo ndiwomwe uli mpingo wanu, inu simukudya pa Mawu.

Izi n’zoonekeratu kuti izi ndi zomwe sankafuna kuti zichitike komanso zomwe anthu anali kuchita.

Ndipo inu muzipita ku tchalitchi; musati mudzikhala kunyumba, kumapita kukawedza, ndi kukasaka, ndi zinthu monga zimenezo Lamlungu.

Ife Sitili. Ife tikulumikizana mozungulira pa chinthu chokhacho chomwe chidzagwirizanitsa Mkwatibwi, Uthenga Uwu, Liwu ili.

Kachiwirinso, Ine ndimakhulupirira kupita kutchalitchi. Pali matchalitchi ambiri kuzungulira padziko lonse lapansi omwe akuika matepi moyambilira pa maguwa awo, Ambuye atamandike. Kodi ine ndikukhulupirira kuti muyenera kukhala panyumba kapena inu simuli Mkwatibwi? AYI, AYI, AYI….ine sindinaganizepo chimenecho, ine sindinakhulupirirepo chimenecho. Ine Ndikungofuna kuti MUZIKANIKIZA KUSEWERA mosatengela kuti kaya inu muli kuti kapena ndi tchalitchi chiti chomwe inu mukupita.

Ngati inu mulibe vumbulutso la zomwe iye akunena, ndiye kuti inu munganene momveka bwino kuti, “Ine Sindiyenera kumvera M’bale Branham ngakhaleso kapena KUVOMEREZA zonse zomwe iye akunena. Ngakhaleso Iye Ananena choncho, pali amuna ena ambiri oitanidwa ndi Mulungu.”

Kazipitaniko. Ife tikuzindikira apa, akuti, “Kodi ife tizipita ku mpingo wina umene sugwirizana ndi inu?” Ndithudi, ine sindi…Ine si nsangalabwi yokhayo mmphepete mwa nyanja, inu mukudziwa. Alipo—alipo amuna ena a umulungu konsekonse; ndikukhulupirira kuti ndine mmodzi wa iwo.

Mawu a Mulungu pa matepi ndiyo SANGALABWI YANGA, THANTHWE LANGA. Ndi Liwu lomwe ndikufuna kumva komanso Liwu lomwe ndikufuna kuti Branham Tabernacle imve.

Ngati inu mukufuna kulumikizana nafe, Inu muli olandiridwa kwambiri, abale ndi alongo anga. Mudzalumikizane nafe Lamlungu nthawi ya 12:00 p.m., nthawi ya ku Jeffersonville, pamene tidzava Liwu la Mulungu likulankhula ndikuyankha mafunso ambiri omwe mungakhale nawo mumtima mwanu. Ndipo mverani nokha ngati zomwe ine ndanena m’kalata iyi sizikugwirizana ndi Mawu ndiso ngati ine sindinamvetse bwino zomwe Mulungu akunena kwa Mkwatibwi Wake.

Zimene iye akunena pa matepi ndi Pakuti Atero Ambuye. Osati zomwe ine ndikunena ndi zomwe iye akunena, kapena zomwe ine ndikukhulupirira kuti iye akunena, ndipo Mulungu YEKHA ndi amene angakupatseni inu Vumbulutso lolondola.

M’bale Joseph Branham

26-0111 Kwawo Kwa Mtsogolo Kwa Mkwati Wa Kumwamba Ndi Mkwatibwi Wa Padziko

Uthenga: 64-0802 Kwawo Kwa Mtsogolo Kwa Mkwati Wa Kumwamba Ndi Mkwatibwi Wa Padziko

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Wanga Kwambiri Wokomamtima.

Ine ndimakukonda iwe kwambiri. Iwe ndiwe mnofu wa mnofu wanga, ndi fupa la fupa langa. Ngakhale ndisanalenge nyenyezi, mwezi, chilengedwe changa chonse, ndinakuona iwe ndipo ndinakukonda iwe kenako. Ndinkadziwa kuti iwe unali gawo la Ine, mmodzi wanga komanso wokomamtima yekhayo. Iwe ndi ine tinali MMODZI.

Tsiku limene ine ndakhala ndikulilakalaka ndi kuliyembekezera kuyambira pamene ndinakuonani inu mapeto ake lafika.Tsopano ine ndikukuitanani inu ndikukugwirizanitsani inu kuchokera kummawa ndi kumadzulo, kumpoto ndi kum’mwera, ndi Liwu Langa. Inu ndinu malingaliro Anga, Mawu Anga, Mkwatibwi Wanga, opangidwa kuwonetseredwa.

Ine ndakhala ndikulakalaka kukuuzani inu chilichonse chomwe chili mumtima mwanga, kotero ine ndinazilemba izo mwa aneneri Anga ndipo ndinasunga Chilichonse kwa zaka zikwizikwi. Ambiri awerenga, ndipo akukhulupirira kwa zaka mazana ambiri, koma ndasunga zinthu zambiri zachinsinsi mpaka INU MUNAFIKA. Ndi inu nokha amene ine ndidzakuuzani.

Iwo ankafunitsitsa kudziwa ndikumva zinthu zodabwitsa zonsezi zomwe ndazisunga mobisa, koma monga momwe ndinakulonjezerani inu, ndakhala ndikuzisunga zachinsinsi mpaka pano, kuti zikhale za INU, MMODZI WANGA KOMANSO YEKHAYO.

Ine ndinakulonjezani inu kuti ine ndikanadzabweranso ndikudziulula ndekha mu thupi la munthu, kuti Ine ndikanakuuzani inu, ndikukuwululirani inu zinthu zonse izi. Ndimafuna kuti inu mumve LIWU LANGA likulankhula kwa inu mwachindunji.

Ine ndadzoza ena ambiri ndi Mzimu Wanga Woyera kuti akuuzeni inu za chikondi Changa, koma monga momwe ine ndakhala ndikuchitira nthawi zonse, ndipo ine sindingakhoze kusinthe, ine ndidasankha munthu m’modzi: Mngelo wanga, mneneri wanga, kuti akhale Liwu Langa kuti Ine ndikhoze kuyankhula Pakuti Atero Ambuye kwa inu.

Ine ndimafuna kukuuzani inu, inu simunapulumutsidwe pa tsiku linalake. Inu Munapulumutsidwa kwa nthawi zonse. Ine ndangobwera kudzakuwombolani inu. Munapulumutsidwa kuchokera pachiyambi chifukwa munali ndi Moyo Wamuyaya kuyambira pachiyambi. Chifukwa chake, m’maso mwanga, machimo anu onse sangawonekereso mpang’ono pomwe kwa ine, chinthu chokhacho chomwe ndimamva ndi liwu lanu. Ndimangoona choyimira chanu.

Momwe Ine ndimafunitsitsa kukuuzani inu zinthu zambiri. Mtima wanga ukudzaza ndi chisangalalo. Momwe Ine Ndikufunitsitsira kukhala ndi Mgonero Wathu wa Ukwati, Zaka Chikwi zathu pamodzi. Kuti ndikuuzeni mwatsatanetsatane zonse zokhudza Kwathu Kwamtsogolo; Momwe ndakukonzerani chilichonse cha inu, ndi chilichonse chokhudza chanu.

Wokomamtima wanga, ngati inu mukuganiza kuti ndi bwino tsopano kumvetsera Liwu Langa likulankhula kwa inu, tangodikirani, uwu ndi mthuzi chabe wa momwe zidzakhalire tikamakakhala mu Mzinda umenewo limodzi. Mneneri wanu adzakhala khomo loyandikira pafupi ndi inu; iye adzakhala wayandikana naye wa inu.

Ife tidzayenda m’misewu yagolide ndikumwa madzi ochokera ku kasupe pamodzi. Tidzayenda kupita ku pamaradaiso a Mulungu ndi Angelo akuzungulira dziko lapansi, kuimba nyimbo za zafuko…Ndi tsiku lotani!

Ine ndikudziwa kuti msewu umaoneka wothyokathyoka, ndipo nthawi zina zimakhala zolimba Kwa inu , koma udzakhala wochepa kwambiri, wochepa kwambiri, pamene tikukhala limodzi wina ndi mzake.

Tsopano, ine kamodzinso ndikusonkhanitsaninso inu ndi kulankhula nanu Lamlungu lino nthawi ya 12:00 PM, nthawi yaku Jeffersonville, ndikukuuzani zonse za “64-0802 Kwawo Kwamtsogolo kwa Mkwati Wa Kumwamba ndi Mkwatibwi Wapadziko Lapansi”. Ine Sindingathe kudikira kuti ndikhale nanu nthawi imeneyo kenako.

Kumbukirani, ndipo musaiwale, ndimakukondani inu kwambiri.

M’malo mwa Iye,

M’bale Joseph Branham

Malemba:
Mateyu Woyera 19:28
Yohane Woyera 14: 1-3
Aefeso 1:10
2 Petro 2: 5-6 / Mutu Wachitatu
Chivumbulutso 2: 7 / 6: 14 / 21: 1-14
Levitiko 23:36
Yesaya Mutu Wachinayi / 28: 10 / 65: 17-25
Malaki 3: 6

26-0104 Zitsime Zong’aluka

Uthenga: 64-0726E Zitsime Zong’aluka

PDF

BranhamTabernacle.org

Okondedwa Iwo Omwa Pa Chitsime Cha Kasupe

Ndi Khirisimasi ndinso Zaka za tsopano zotani zomwe ife takhala tili nazo. Talandira ndikutsegula mphatso za Mulungu zomwe adatumiza kwa Mkwatibwi Wake. Mphatso yathu yoyamba inali Mphatso yayikulu kwambiri ya Khirisimasi yomwe idakulungidwapo. Mulungu Mwiniwake adakulunga Iye mwini mu thupi la munthu ndipo adatumiza phukusi limenelo kudziko lapansi. Inali Mphatso Yake yoyamba yayikulu yobwezeretsa Mkwatibwi Wake.

Kenako Mulungu adatumiza phukusi lina lalikulu kwa Mkwatibwi Wake. Iye Anatikonda ife kwambiri kotero kuti Iye anabwera nadziulula Yekha mu thupi kachiwiri kuti Iye athe kulankhula nafe pakamwa ndi Kupita ku khutu. Anafuna kuti Iye ndi Mkwatibwi Wake akhale Mmodzi.

Ndipo tsopano, abwenzi, musati mundive ine molakwika.Ine nditi ndinene izi ndi ulemu mumtima mwanga, podziwa kuti ndine munthu womangirilidwa ku Kumuyaya amene ndidzayima mu mchiweruzo tsiku lina: Anthu zikwizikwi akuyiphonya mphatso yawo. Mukuona? Iwo sangathe kuyimvetsa iyo. Ndipo iwo akuyiyang’ana, ndipo nanena, “O, iye ndi munthu chabe.” Izo Ndi zoona. Kodi iye anali Mulungu kapena Mose amene anapulumutsa anthu? Iye anali Mulungu mwa Mose. Mukuona? Iwo Analirira kwa mpulumutsi. Ndipo pamene Mulungu anatumiza mpulumutsi kwa iwo, iwo analephera kuchiwona icho, chifukwa icho chinali mwa munthu, koma sanali munthuyo, anali Mulungu mwa munthuyo.

Lero, kachiwiri, anthu zikwizikwi akuyiphonya mphatso yawo ndipo akunena kuti, “Inu simukuyenera kumvera matepi, tsopano pali amuna ena odzozedwa,” zomwe ndi zoona, koma iwo akulephera kuzindikira kuti ilo ndi Liwu LOKHALO lotsimikiziridwa ndi Mulungu , likulankhula Pakuti Atero Ambuye kudzera mwa munthu ameneyo. Liwu limenelo ndi Yurimu Tumimu wa Mulungu, Mtheradi Wake wa lero.

Pamene ife tikumvetsera Liwu Lake pa matepi ife kwenikweni timakhala kuti tikumwa kuchokera ku Chitsime cha Kasupe wa Mulungu, chomwe sichifuna sichifuna kupopa, sichifuna kukoka, sichifuna kujoyina, kapena sichifuna kugwedeza; ife tikungokhulupirira ndi kupumula pa Mawu aliwonse olankhulidwa.

Pa kumvetsera Liwu limenelo pa matepi, malingana ndi Yesu Mwiniwake, ife tili nawo umboni weniweni wa Mzimu Woyera mtsiku lathu.

Kotero pamenepo pali umboni weniweni wa Mzimu Woyera! Iye sanayambe wandiuzapo ine chirichonse cholakwika panobe. Iwo, “Uli umboni wa Mzimu Woyera, ndi iye yemwe angakhoze kukhulupirira Mawu, ngati inu mungakhoze kuwalandira Iwo.

Mulungu wapereka Kasupe amene ife tingamwe kuchokera Kwa iye mphindi iliyonse ya tsiku lililonse. Nthawi zonse amakhala watsopano. Si chinthu chinachake choyima, Iye ndi Kasupe Wake wosaguga, wodzithandizira yekha; inu mukungoyenera Kukanikiza kungosewera.

Kunena za MPHATSO yochokera kwa Mulungu, kodi inu mungaganizire momwe Mphatso iyi kwenikweni ili YAIKULU? Mu mkuphweka pa Kukanikiza kungosewera ndi kumvetsera ku Liwu Lake pa matepi, ndiye lokhalo…LIWU LOKHALO padziko lapansi lomwe inu simukufunaso fyuluta, sefa, kapena china chilichonse.Inu muyenera kungomvetsera, kukhulupirira, ndi kunena ameni ku Mawu onse.

Mulungu mwiniwake wapereka njira iyi, NJIRA YAKE YOKHAYO, yolandililako moyo wosatha, komanso ngakhale chofunika kwambiri, KUKHALA MKWATIBWI WAKE. Tikhoza kungogona pachifuwa Chake ndi kuyamwa mphamvu zathu pomvera Kasupe Wake, Liwu Lake, El Shaddai akulankhula ndi Mkwatibwi Wake.

Chaka chino chikhale chaka chomwe Iye akubwera kwa ife, Mkwatibwi Wake wokondedwa. Ife Tikuyang’anira ndi kuyembekezera ndi chiyembekezo chachikulu. Tsiku lililonse tsopano tidzayang’ana omwe takhala tikulakalaka kuwawona akuwonekera. Ife Tidzazindikira, mu mkutwanima Kwa diso chabe, kuti tidzachoka pano, kuyitanidwa ku Mgonero Wathu wa Ukwati.

Ambuye, pamene ife tidzawona gome lalikulu ilo litayikidwa kunja uko, ku mgonero umenewo, mailosi zikwi utali wake; kuyang’anizana pa gomelo kwa wina ndi mzake, ankhondo akale a zipsyera, misozi ya chimwemwe ikutsikira pansi pa masaya athu. Mfumu kutulukira uko, kukongola Kwake, chiyero, kuyendera pansi motsatira gomelo, ndi kutenga manja Ake Omwe ndi kumaipukuta misonzi kuichotsa pa maso awo, akuti, “Musati muziliranso. Zonse zatha. Lowani mu zisangalalo za Ambuye.” Zovutikira za ulendo sizidzawoneka ngati kanthu pamenepo, Atate, pamene ife tidzafika pa mapeto a ulendo.

Bwerani ndipo mudzamwe, mudzamwe ndipo mudzamwe kuchokera ku Kasupe woperekedwa ndi Mulungu lero ndi ife Lamlungu lino nthawi ya 12:00 PM, nthawi ya ku Jeffersonville. Iwo ndi malo okhawo omwe inu mungathe kupumulirako mokwanira ndikunena AMEN ku Mawu aliwonse omwe mukumva. Ndi chitsime chake cha Kasupe choperekedwa kwa Mkwatibwi Wake kuti amwe kuchokera ku icho.

M’bale Joseph Branham

Uthenga: 64-0726E Zitsime Zong’aluka
Malemba oti muwerenge musanamve Uthenga:
Masalmo 36:9
Yeremiya 2:12-13
Yohane Woyera 3:16
Chivumbulutso Mutu 13

25-1228 Kuzindikira Tsiku Lanu Ndi Uthenga Wake

Uthenga: 64-0726M Kuzindikira Tsiku Lanu Ndi Uthenga Wake

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mkwatibwi Wodulidwa,

Lero lino, mpingo wayiwala mneneri wawo. Iwo Samufunanso Iye mpang’ono pomwe kuti azilalikira m’matchalitchi awo. Iwo amanena kuti ali ndi abusa awo kuti aziwalalikira iwo ndi kumatchula mobwereza mawu ndi kumasulira Mawu. Kulalikira n’kofunika kwambiri kuposa kumvetsera liwu la Mulungu pa matepi m’matchalitchi awo.

Koma Mulungu Iye ankadziwa kuti ankayenera kukhala ndi mneneri Wake; mmenemu ndi momwe nthawi zonse Iye amaitanira ndi kutsogolera Mkwatibwi Wake. Iye anatidula kuchokera m’mitundu yonse ndi Lupanga Lake lakuthwa konsekonse, Mzimu Wake Woyera, Liwu Lake loyankhulidwa ndi mneneri Wake.

Iye watidula ife ndi Liwu limenelo. Ndicho chifukwa chake Iye analijambula ilo ndi kuliyika pa tepi. Mwa Vumbulutso ife timawona momwe Malemba alili angwiro! Mkwatibwi sangache pokhapokha Mwana atamuchetsa iye.

Ziribe kanthu ndi mochuluka bwanji momwe inu mungalalikire, chirichonse chimene inu mungachite, icho sichingakhoze kucha, icho sichingawonetseredwe, icho sichingatsimikiziridwe; kokha ndi Iye Amene anati, “Ine ndine Kuwala kwa dziko lapansi,” Mawu.

Mawu adatiuza ife kuti Mzimu Woyera mwiniwake adzabweranso ndi kudzatichetsa ife, kudzatsimikizira, kudzasonyeza umboni ndi kudzadzipanga Iyemwini kudzadziwonetsera. Kuwala kwamadzulo kwafika. Mulungu akudzionetsera yekha mu thupi kuti ayitane Mkwatibwi Wake.

Iye ndiye amene wakuitanani INU ndi Mzimu Wake Woyera, Mawu Ake, Liwu lake. Iye ndiye amene anakusankhani INU. Iye ndiye amene akukuphunzitsani INU. Iye ndiye amene akutsogolerani INU. Ndi chiyani? Mzimu Wake Woyera, Liwu Lake likuyankhula MWACHINDUNJI KWA INU.

Koma izo ndi zakale kwambiri kwa iwo lero lino. Iwo sangakhoze kusewera matepi m’matchalitchi awo. Iwo Sakuzindikira. Ndicho chifukwa chake ali mu mkhalidwe womwe ali. Koma kwa inu, izo zawululidwa kuti ndi njira yoperekedwa ndi Mulungu, IZO NDI PAKUTI ATERO AMBUYE KWA INU.

Chotero pakuyenera kubwera a—a—a Mphamvu, Mzimu Woyera Mwiniwake, kuti udzachetse, kapena kutsimikizira, kapena kudzatsimikizira, kapena kudzawonetsera icho chimene Iye ananeneratu kuti chikanadzachitika mu tsiku lino. Kuwala kwa kumadzulo kukupanga zimenezo. Ndi nthawi yotani!

Ife ndife Mkwatibwi wangwiro wa Mawu a Mulungu amene mneneri wake anaona mu masomphenya. Ife ndiwo amene Iye anatumiziridwako mneneri wake kuti awaitane ndi Mawu ake, ndipo iwo tsopano akukhala ndi CHITSITSIMUTSO, chifukwa tsopano ife tikudziwa chimene ife tiri.

Kutsitsimutsa, apo, ndi mawu omwewo amene amagwiritsidwa ntchito kwina kulikonse, ine ndinangowayang’ana iwo, amatanthauza, “chitsitsimutso.” “Iye adzatitsitsimutsa ife akadzatha masiku awiri.” Izo zidzakhala, “Patsiku lachitatu Iye adzatitsitsimutsanso ife, Iye atatibalalitsa ife, ndi kutichititsa khungu, ndi kuting’amba ife.”

Atate anatuma mneneri wake kuti ayang’anire Mkwatibwi wake kuti tisachoke pa mzere. Kumbukirani, awa anali masomphenya!

Mkwatibwi anadutsa malo omwewo amene Iye anali pamene Iye anali pachiyambi. Koma ine ndinali kumuwona Iye akuchoka pa sitepe, ndi kumayesera kumukokera Iye mmbuyo.

Koma kodi “iye” angamukokere m’mbuyo bwanji lero? “Iye”, mwamunayo, sali pano padziko lapansi. NDI MAWU! Kodi Mawu OKHA Otsimikiziridwa a lero ndi ati? Liwu la Mulungu pa matepi.

Atumiki ai oyitanidwa kulalikira Mawu potchula mobwera zomwe mneneriyo ananena. Malinga ndi mneneri mwiniwake, iwo sayenera kunena china chilichonse mochuluka

Zoonadi, aIi oyitanidwa kuphunzitsa ndi kulalikira Mawu amenewo. Koma pali LIWU LIMODZI LOKHA LOMWE NDILOTSIMIKIZIRIDWA NDI MULUNGU IYEMWINI KUTI NDILO PAKUTI ATERO AMBUYE.

Chotero ine ndikunena, mu Dzina la Yesu Khristu! Musati inu muwonjezere kanthu kamodzi. Musati mutenge, kuyika malingaliro anu omwe mwa Iwo. Inu muzingonena chimene chikunenedwa pa matepi awo. Inu muzingochita chimodzimodzi chimene Ambuye Mulungu wakulamulirani kuti muchite. Musati muwonjezere kwa Iwo.

Ngati inu munena kuti “ameni” pa mawu aliwonse amene m’busa wanu kapena mtumiki wanu akunena, inu mwatayika. Koma ngati munena kuti “AMENI” PA MAWU ALIWONSE AMENE MULUNGU ANAYANKHULA KUDZERA MWA MNENERI WAKE PA MATEPI, INU NDINU MKWATIBWI NDIPO MUDZAKHALA NDI MOYO WOSATHA.

Mneneri wa Mulungu anali munthu amene Mulungu anasankha kulankhula kudzera mwa iye. Kunali kusankha Kwa Mulungu kumugwiritsa ntchito iye kulankhula Mawu Ake ndikuwayika pa matepi kuti Mkwatibwi nthawi zonse akhale ndi PAKUTI ATERO AMBUYE WOTI AZIMVERA.

Iye sakufuna kuti Mkwatibwi Wake azidalira zomwe anthu ena akunena, kapena kutanthauzira kwawo Kwa Mawu Ake. Iye akufuna kuti Mkwatibwi Wake azimva kuchokera pakamwa pake kupita m’makutu mwawo. Iye sakufuna kuti Mkwatibwi Wake azidalira wina aliyense koma Iyemwini.

Ife tikadzuka m’mawa, timakonda iye kuti atiuze ife kuti, “Mmawa wabwino abwenzi. Ine Ndilankhula ndi inu lero ndikukuuzani momwe ine ndimakukonderani inu komanso momwe inu ndi ine tili AMODZI. Ndili ndi ambiri omwe ndidzawapatse moyo wosatha, koma INU nokha ndinu Mkwatibwi wanga wogwiridwa pa dzanja. INU nokha ndi amene ine ndapereka Vumbulutso maziko adziko asanakhazikitsidwe .

Ambiri amakonda kundimva, koma ine ndakusankhani inu kuti mukhale Mkwatibwi Wanga. Pakuti mwandizindikira Ine ndipo mwakhala ndi Mawu Anga. Inu Simunanyengerere, simunasewere, koma mwakhalabe okhulupirika ndi Mawu Anga.

Nthawi yayandikira. Ndikubwera kudzakutengani posachedwa. Choyamba, mudzawona omwe ali kale ndi ine tsopano. O, momwe iwo akufunira kukuonani inu ndikukhala nanu. Musadandaule ana aang’ono, chilichonse chili pa nthawi yake, basi pitirizani kumenyera.”

Monga mtumiki wa Uthenga, ine sindingathe kuwona chinthu chimodzi chatsalira koma kupita kwa Mkwatibwi.

M’bale Joseph Branham

Uthenga: 64-0726M “Kulizindikira Tsiku Lanu ndi Uthenga Wake”
Nthawi: 12:00 P.M., nthawi ya ku Jeffersonville

Malemba oti muwerenge musanamve Uthenga:
Hoseya: Chaputala 6
Ezekieli: Chaputala 37
Malaki: 3:1 / 4:5-6
II Timoteo: 3:1-9
Chivumbulutso: Chaputala 11

25-1221 Kupita Kuseri Kwa Msasa

Uthenga: 64-0719E Kupita Kuseri Kwa Msasa

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Wachikondi,

Mulungu samasintha. Mawu Ake samasintha. Pulogalamu yake simasintha. Ndipo Mkwatibwi Wake samasintha, Ife tidzakhala ndi Mawu. Iwo ndi oposa moyo kwa ife; iwo ndi Kasupe wa Madzi amoyo.

Chinthu chokha chomwe ife tapatsidwa ntchito ndikumva Mawu, omwe ndi Mawu a Mulungu otsimikiziridwa omwe adajambulidwa ndikuyikidwa pa matepi. Chinthu chokha chomwe timawona si chikhulupiriro, osati gulu la amuna, sitiwona china chilichonse koma Yesu, ndipo Iye ndiye Mawu opangidwa kukhala thupi mu masiku athu ano.

Mulungu ali mu Msasa wathu ndipo tili panjira yopita ku Ulemerero motsogozedwa ndi Lawi la Moto, lomwe ndi Mulungu Mwiniwake akulankhula kudzera mwa mneneri wake wotsimikiziridwa wa Malaki 4. Tikudya Mana wobisika, Madzi amoyo omwe Mkwatibwi yekha ndi amene angadye.

Mulungu sasintha njira zake, koteroso mdierekezi sasintha njira zake. Zimene adachita zaka 2000 zapitazo, akuchita zomwezo lero, kupatula kuti ali wa mphavu kwambiri.

Tsopano, zitatha zaka foro handiredi, Mulungu anadzayenda kumene pakati pawo tsiku lina. Molingana ndi Lemba, Iye anali woti adzasandulike thupi ndi kudzakhala pakati pawo. “Dzina Lake azidzatchedwa Wauphungu, Kalonga wa Mtendere, Mulungu Wamphamvu, Atate Wosatha.”
Ndipo pamene Iye anadzabwera pakati pa anthuwo, iwo anati, “Ife sitimulola kuti Munthu uyu azitilamulira ife!

Potengela ndi Malemba, Mwana wa Munthu adzabweranso ndi kukhala ndi moyo ndi kudziulula Yekha mu thupi la munthu, ndipo Iye anachitadi zimenezo, ndipo iwo akunena zomwezo. Inde, iwo amakamba mobwereza ndi kulalikira Uthenga, koma Iwo samalola munthu ameneyo kuwalamulira iwo.

Izi ndizo kwenikweni zomwe zili kuchitika :

Ndipo monga zinaliri kumeneko, chomwechonso izo ziri tsopano! Baibulo linati mpingo wa Laodikaya ukanadzamuika Iye panja, ndipo Iye anali akugogoda, akuyesera kuti alowe mkati. Pali chinachake cholakwika penapake.
Tsopano, bwanji? Iwo anali atapanga msasa wawo wawo.

Munthu anganene kuti, “Ine ndikudziwa ndipo ine ndimakhulupirira kuti M’bale Branham anali mneneri. Iye anali mngelo wachisanu ndi chiwiri. Iye anali Eliya. Timakhulupirira Uthenga uwu. Kenako iye ndikupanga mtundu wina wakunyozela, Iwo angakhale uliwonse womwe ulipo, osasewera Liwu LOKHA LOTSIMIKIZILIDWA la Mulungu mu mpingo wawo… Pamenepo pali chinachake cholakwika penakwake. Tsopano, ndi chifukwa chiyani? Iwo adapanga msasa wawo.

Ine ndikunena zinthu izi kuti osati kuti tilekanitse mpingo iyayi, Mawu a Mulungu ndi emene amachita zimenezo. Ine ndikufuna kuti ife tonse tigwirizane pamodzi, tikhale CHINTHU CHIMODZI wina ndi mnzake komanso ndi Iye, koma pali njira imodzi yokha yochitira zimenezo: mozungulira Liwu la Mulungu pa matepi. Ameneyo ndiye PAKUTI ATERO AMBUYE YEKHA WA MULUNGU.

Mulungu wavumbulutsira njira Yake yangwiro kwa ife. Iyo ili yaulemerero kwambiri ndiposo yosavuta. Uthenga uliwonse umene timamumva Iye akutiuza, kutitsimikizira, kutilimbikitsa, kuti NDIFE MKWATIBWI WAKE. Tili mu chifuniro Chake changwiro. Tadzipanga ife eni kudzikonzekeretsa tokha pa KUMUNVA IYE

Uthenga uwu uli watsopano kwambiri kuposa nyuzipepala ya mawa. Ndife ulosi womwe ukukwaniritsidwa. Ndife Mawu owonetseredwa. Mulungu amatitsimikizira ndi Uthenga uliwonse umene timamva kuti tsiku ili lero , Lemba ili likukwaniritsidwa.

Pakhoza kukhala ena uko kudutsa mafuko, kuzungulira dziko, amene ngakhale tepi iyi idzakawapeza mmakomo mwawo kapena mmatchalitchi mwawo. Ife tikupemphera, Ambuye, kuti pamene msonkhano ukupitirira, pa—pa…kapena tepiyo izikaseweredwa, kapena pamalo amene tingadzakhale tiripo, ka—kapena chikhalidwe, mulole Mulungu wamkulu wa Kumwamba mulemekeze kudzipereka uku kwa mitima yathu mmawa uno, ndipo muchiritse osowa, mupereke kwa iwo zimene iwo akuzisowa.

Dikirani chabe mwa ka mphindi ….Kodi Liwu la Mulungu kwa dziko lapansi linalosela ndi kunena chiyani?….anthu azizasewera matepi m’nyumba zawo kapena m’matchalitchi awo.

Koma ife tikutsutsidwa ndi kudzudzulidwa ponena kuti ife SITINGAKHALE NDI Tchalitchi cha Tepi Cha mnyumba? Kodi M’bale Branham sananenepo kuti muzisewera matepi m’matchalitchi anu?

ULEMERERO KWA MULUNGU, IMVETSENI IYO, WERENGENI IZO, IZO NDI PAKUTI ATERO AMBUYE. Ndipo sikuti Iye anangonena izi zokha, komanso posewera matepi m’nyumba zanu ndi m’matchalitchi, Mulungu wamkulu wa Kumwamba adzalemekeza kukhulupirika kwa mitima yathu ndikuchiritsa osowa ndikutipatsa ife CHILI CHONSE CHOMWE TIKUFUNA!!

Chobwerezedwa ichi chimodzi chokhachi CHIKUTSIMIKIZIRA kuti anthu akumvetsera abusa awo ndipo iwo SAKUMVA MAWU, kapena Iwo angawatsutse ndikuwatsimikizira ndi MAWU kuti ife tili mu CHIFUNIRO CHAKE CHANGWIRO, ndipo ndi CHIFUNIRO CHAKE CHANGWIRO KUSEWERA MATEPI M’MATCHALITCHI AWO.

Sindikusokeretsa kapena kubwereza mawu molakwika Mawu monga momwe ambiri amanenera. Imvereni ndipo muwerenge izo nokha.

Ndipo ndi zophweka komanso zangwiro, INGOKANIKIZANI KUSEWERA ndipo mumve Liwu la Mulungu likulankhula nanu. Nenani “Amen” ku Mawu aliwonse omwe inu mukumva. Inu Simuyenera konse kuwamvetsa, inu muyenera kokha kungokhulupilira izo.

“Ine ndikufuna kuti ndipite opanda msasa. Ziribe kanthu kuti ine ndilipira chiyani, ine nditenga mtanda wanga ndipo ndiziunyamula iwo tsiku ndi tsiku. Ine ndipita mopitirira msasa. Ziribe kanthu kuti anthu azinena chiyani za ine, ine ndikufuna kuti ndizimutsatira Iye kunja kwa msasa. Ine ndakonzeka kuti ndizipita.”

Bwerani ndipo mudzapite mopitilira chotchinga cha mawu kupita ku Mawu a Mulungu Lamlungu lino nthawi ya 12:00 PM, nthawi ya ku Jeffersonville. Izo zilibe malire zomwe Mulungu angachite ndiso zomwe adzachita ndi munthu amene ali wokonzeka kupita mopitirira msasa wa anthu.

M’bale Joseph Branham

Uthenga: 64-0719E Kupita Mopitilira Msasa

Malemba Opatulika: Ahebri 13:10-14 / Mateyu 17:4-8

25-1214 Phwando La Malipenga

Uthenga: 64-0719M Phwando La Malipenga

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mkwatibwi Wangwiro

Izi sizongozipanga, abwenzi. Izi ndi PAKUTI ATERO AMBUYE, Lemba.

Mkristu aliyense amafuna kukhala Mkwatibwi, koma tikudziwa kuti Mkwatibwi Wake adzakhala okhawo osankhidwa ake ochepa . Tikudziwa kuti Iye ali ndi chifuniro chongololera, koma Mkwatibwi Wake ayenera kukhala mu chifuniro chake changwiro. Kotero, ife tiyenera kufunafuna Mulungu mu Mawu Ake, ndipo kenako mwa vumbulutso, ife tidzadziwa chifuniro Cha Iye changwiro momwe ife tingakhalire Mkwatibwi Wake.

Ife tiyenera kufufuza lemba, chifukwa tikudziwa kuti Mulungu SAMASINTHA malingaliro Ake pa Mawu Ake. Mulungu sasintha pologaramu yake.Iye Sasintha CHILICHONSE. Momwe Iye anachitira izo nthawi yoyamba ndi wangwiro. Zimene Iye anachita dzulo Adzachitanso chimodzimodzi lero.

Momwe Iye anapulumutsira munthu kuyambira pachiyambi, Iye ayenera kupulumutsa munthu lero mwanjira yomweyo. Momwe Iye Anachiritsira munthu woyamba, Iye ayenera kuchita chimodzimodzi lero. Momwe Mulungu anasankhira kuyitana ndi kutsogolera Mkwatibwi Wake, Iye Adzachita chimodzimodzi lero; pakuti Iye ndi Mulungu ndipo sangasinthe. Mawu amatiuza kuti Yesu Khristu ali YEMWEYO dzulo, lero ndi kwanthawi zonse.

Kotero, Ife tikamawerenga Mawu Ake, timatha kuona bwino lomwe momwe Iye anasankhira kuyitana ndi kutsogolera Mkwatibwi Wake pa nthawi iliyonse. Adasankha MUNTHU MMODZI. Iye anati iwo anali Mawu a tsiku lawo. Mneneri anatiuza Ife kuti Iye SANALI ndi gulu la amuna; Iwo amakhala ndi njira zosiyanasiyana, malingaliro osiyanasiyana, ndipo chofunika kwambiri, Iye anati, MAWU A MULUNGU SAMAFUNIKA KUTANTHAUZIRA.

Ndiye, zomwe mneneri aliyense adalankhula mu mbadyo uliwonse sizingawonjezeredwepo kapena kuchotseredwapo. Ziyenera kukhala Mawu pa Mawu zomwe IYE ANALANKHULA. Zophweka kwambiri ngati Inu mundifunsa ine kuti nanga njira yoperekedwa ndi Mulungu ndi iti….KHALANI NDI MNENERI.

Tsopano, ife sitikungodziwa kokha kwenikweni yomwe yakhala ili njira yoperekedwa ndi Mulungu kuyambira pachiyambi, Ambuye adzalankhula ngakhale kudzera mwa mngelo wake ndikutiuza zomwe Iye adzachita mtsogolo, kuti basi adzatsimikizire kachiwiri, MULUNGU SAMASINTHA DONGOSOLO LAKE.

Mkwatibwi Wake (ife) titachoka padziko lapansi lino ndikuyitanidwa ku Mgonero wa Ukwati, kodi Mulungu adzaitana bwanji Ayuda osankhidwa 144,000? Gulu la amuna?

Ndipo pa nthawi yomweyo…Tsopano, mwamsanga pamene Mpingo uwu (Mkwatibwi) ukusendezedwa pamodzi, Iwo ukutengedwera mmwamba; ndipo chinsinsi icho cha Chisindikizo cha Chisanu ndi chiwiri, kapena Chisindikizo cha Chisanu ndi chiwiri, chinsinsi cha kupita. Ndipo Ayuda akuitanidwa ndi chinsinsi cha Lipenga la Chisanu ndi chiwiri, chimene chiri aneneri awiri, Eliya ndi Mose, ndipo iwo akubwereranso.

Kotero Mkwatibwi akusendezedwa pamodzi, ife tidzatengedwera mmwamba. Ife Tikudziwa kuti pali chinthu chimodzi chokha chomwe chingamusendeze Mkwatibwi pamodzi, Mzimu Woyera, ndipo Mzimu Woyera ndi Mawu Ake, ndipo Mawu Ake a lero ndi Liwu la Mulungu, ndipo Liwu la Mulungu ndi…

Ngati ine ndidakukhumudwitsani Inu pa kunena zimenezo, mundikhululukire ine, koma, ndinaverera kuti mwina icho chidazembedwa, koma, Ine ndine Liwu la Mulungu kwa inu. Mukuona? Ine Ndikunenanso zimenezo kachiwiri, nthawi imene ija ndidali pansi pa kudzoza, Inu mukuona.

Ndingolankhula ine pomwe pano ndi kunena kuti, CHOBWEREZA CHIMODZI chokha ichi chochokera kwa mthenga wa mngelo wotsimikiziridwa wa Mulungu chiyenera kukhala chokwanira kwa onse odzitcha okhulupirira mu Uthenga wa nthawi yotsiriza uwu kuti apemphe abusa awo kuti azikanikiza kusewera m’matchalitchi awo kapena kuti achoke pa udindo kuti iwo asankhe m’busa wokhala ndi VUMBULUTSO LENI LENI LOCHOKERA KWA MULUNGU.

Choncho, Lipenga linamveka ndipo aneneri awiri awa akuwonekera chifukwa Iye sangakhale ndi mngelo wake wachisanu ndi chiwiri ndi Mkwatibwi wake pano padziko lapansi nthawi yomweyo yomwe akubwera. Ndiye kodi Iye akuwayitani bwanji Ayuda? Mwanjira yofanana momwe Iye anamuyitanila Mkwatibwi wake wa Amitundu.

Ndipo Ayuda akuitanidwa ndi chinsinsi cha Lipenga Lachisanu ndi chiwiri, chomwe ndi aneneri awiri…

Mkwatibwi ayenera kuti achokepo pa njirayo, kuti azipita mmwamba tsopano; kuti antchito awiriwo, antchito awiri awo a Mulungu, mu Chivumbulutso, aneneri awiriwo, akhoza kuwonekera poyera, kuti adzawombe Lipenga la Chisanu ndi chiwiri kwa iwo, kumudzindikiritsa kwa iwo Khristu.

Zomveka bwino kwambiri, Mulungu sasintha dongosolo lake.Iye anatumiza aneneri Ake. Motero, Mkwatibwi Wake adzakhala ndi njira Yake yoperekedwa, mneneri Wake wa angelo, Liwu la Mulungu pa matepi.

Kenako kuti izo zimveke bwino, Mulungu kachiwiri akulankhulanso ndikumuuza Mkwatibwi Wake kuti: Mwakhala okhulupirika kwa Ine ndi njira Yanga yoperekedwa, kotero njira Yanga yoperekedwa ya tsiku lanu idzayankhula kwa inu:

Mngelo wachisanu ndi chiwiri, mtumiki, akuti, “Taonani Mwanawankhosa wa Mulungu amene akuchotsa tchimo la dziko lapansi!”

Kotero lofunikira kwambiri ndi LIWU LIMENELO; LIWU LA MULUNGU akulankhula kudzera mwa mngelo wake wachisanu ndi chiwiri pa matepi. Mulungu adzagwiritsa ntchito MAWU AMENEWO, LIWU LA M’NGELO WAKE WACHISANU NDI CHIWIRI. OSATI GULU…OSATI INE…OSATI M’BUSA WANU…LIWU LA MTUMIKI WAKE WA MNGELO WACHISANU NDI CHIWIRI kuti atidziwitse ife kwa Iye, Ambuye wathu Yesu Khristu.

Motero, ife tikudziwa:

• IFE NDIFE MKWATIBWI WAKE.
• IFE TILI MU CHIFUNIRO CHAKE CHANGWIRO.
• IFE TIKUTSATIRA DONGOSOLO LAKE LA TSIKU LA LERO PAKUKANIKUZA KUSEWERA.

Gawo la Mkwatibwi Wake lidzakhala likusonkhana Lamlungu lino nthawi ya 12:00 PM, nthawi ya ku Jeffersonville, kumvetsera m’busa wathu, mthenga wa mngelo wa Mulungu, William Marrion Branham, ndipo Iye adzalankhula ndi kutiululira kuti palibe mpingo wina, palibe gulu lina la anthu kuyambira chikhazikitsidwire kwa dziko lapansi, lomwe lakhala ndi mwayi woti ife tigwirizane pamodzi kumvetsera Mulungu akulankhula mwachindunji ndi iwo.

Ndi anthu odala bwanji ife. Ife Ndi okondwa kwambiri. Ife kotero ndi oyamikira kwambiri . Mkwatibwi akukhala MMODZI ndi Mkwati.

M’bale Joseph Branham

Uthenga: Malipenga A Phwando 64-0719M.

Malemba oti muwerenge musanamve Uthenga:

Levitiko 16
Levitiko 23:23-27
Yesaya 18:1-3
Yesaya 27:12-13
Chivumbulutso 10:1-7
Chivumbulutso 9:13-14
Chivumbulutso 17:8

25-1207 Kenako Yesu Anabwera Ndipo Anadzaitana

Uthenga: 64-0213 Kenako Yesu Anabwera Ndipo Anadzaitana

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mkwatibwi wa Mawu,

Tikukhala mu nthawi yamdima kwambiri, koma tilibe MANTHA, Ambuye wabwera. Wabwera kudzakwaniritsa Mawu Ake mu tsiku lomaliza. Chimene Iye anali panthawiyo, Iye ali lero. Chimene kuonekera kwake ndi kudziwika kwake zinali, ndi lero. Iye akadali Mawu a Mulungu, akudziwonetsera Yekha mu thupi la munthu mwa mngelo wake wachisanu ndi chiwiri wamphamvu ndipo watiululila ife, ife ndife Mkwatibwi wake wa Mawu a moyo.

Tilibe nthawi ya mtsutso kapena mkangano; Ife tinadutsa tsiku limenelo; tikupita patsogolo, Ife tikuyenera kukafika kumeneko. Mzimu Woyera wabwera pakati pathu. Ambuye Yesu mu mawonekedwe a Mzimu wadziulula ndi kudziwonetsera Yekha kudzera mwa mneneri Wake kuti Iye ndi Liwu la Mulungu kwa Mkwatibwi Wake.

Iye anati adzabwera. Iye anati adzachita izi. Iye anati adzauka m’masiku otsiriza ndikuchita zinthu izi monga momwe Iye anachitira pamene anabwera m’thupi nthawi yoyamba, ndipo apa akuchita izi. Kodi inu mukuopa chiyani? PALIBE!!!

Tili pa njira ya kwathu yopita ku Ulemerero! Palibe chomwe ife chingatilepheretse. Mulungu adzatsimikizira Mawu Ake. Sindikusamala zomwe zikuchitika. Nthawi yafika yochitapo kanthu. Nthawi yafika yo khulupilira kapena kusakhulupirira. Mzere uja wolekanitsa umene umabwera kwa mwamuna ndi mkazi aliyense wafika.

Inu Munabadwira pa cholinga. Pamene Kuwala kunakukanthani inu, Kunachotsa kudetsedwa konse mkati mwa inu. Pamene munamva Liwu Lake likulankhula ndi inu pa matepi, chinachake chinachitika. Kunalankhula ndi moyo wanu. Kunati, “Ambuye wabwera ndipo akukuitanani inu. Musatope, musaope, Ine ndikukuitanani inu. Ndinu Mkwatibwi Wanga”.

Oh Anthu inu, onetsetsani! Musamangotenga chatheka chilichose pa izo. Mulungu ali ndi pologaramu: Mawu Ake Iye adawajambula pa matepi. Ambuye wabwera ndipo akukuitanani inu. Bwerani ku njira yoperekedwa ndi Mulungu.

Ambuye adzagwirizanitsanso Mkwatibwi Wake padziko lonse lapansi ndi Liwu Lake. Adzatilimbikitsa ife, kutitsimikizira ife, kutichiritsa ife, kutibweretsa mu mKukhalapo Kwake kwamphamvu ndikutiuza ife:

Mbuye wabwera ndipo Iye akuitana iwe. Oh, wochimwa, oh, munthu wodwala, kodi iwe sukuwona Mbuye akuwonetseredwa mwa anthu, pakati pa okhulupirira? Iye wabwera kuti adzaitane ana Ake okhulupirira kuti akhale athanzi. Iye wabwera kuti adzamuitanire wochimwa ku kulapa. Wobwerera mmbuyo, membala wa mpingo, Mbuye wabwera ndipo akukuitanani inu.

Kodi ndikutsanyulila kotani Kwa mzimu woyera komwe mkwatibwi adzakhale nako Lamlungu lino pamene Mulungu akusonkhanitsaso ana ake pamodzi kachiwiri ndi kulowa m’nyumba zathu, m’matchalitchi athu, m’misonkhano yathu, ndikutiyitana ife kunena kuti, “Ambuye wabwera ndipo akuitana. Chilichonse chomwe Inu mukuchifuna, ndi chanu.”

Lolani mawu amenewo alowe mozama m’mitima mwanu, abale ndi alongo. CHILICHONSE CHIMENE INU MUKUFUNA, AMBUYE WABWERA NDIPO APEREKA ICHO KWA INU.

Atate Akumwamba, O Ambuye, mulole izo zichitikenso. Zinthu zonse izi zimene ine ndanena, “Yesu wabwera ndipo akukuitanani inu.” Kodi Iye akuchita chiyani pamene Iye wabwera? Iye akuitana. Ndipo mulole izo zichitikenso, Ambuye. Mulole Mzimu Woyera Wanu ubwere pakati pa anthu usikuuno, Ambuye Yesu mu mmaonekedwe a—a Mzimu. Mulole Iye abwere usikuuno ndipo adzadziulule Yekha, ndipo potero adzadziwonetsere Yekha.

M’bale Joseph Branham

Uthenga: Kenako Yesu Adabwera Ndipo Adayitana
Nthawi:12:00 PM nthawi ya ku Jeffersonville
Malemba: Yohane Woyera 11:18-28