All posts by admin5

25-1109 Chosamvetseka

Uthenga: 64-0614E Chosamvetseka

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mulungu Wokhala Ndi Chikopa Pa Iye.

Ife Sitili kuseri kwa chophimba tsopano, ana aang’ono, Mulungu wabwera powonekera bwino kwa ife. Mulungu wamphamvu wa Kumwamba ndi dziko lapansi, Amene nthawi zonse wakhala akudziphimba kwa anthu monga Lawi la Moto lomwe linachokera kwa Mulungu ndikukhala m’thupi la padziko lapansi lotchedwa Yesu; kenako anabwerera ku Lawi la Moto ndipo anaonekera kwa Paulo panjira yopita ku Damasiko, tsopano wabweranso powonekera bwino ndipo anakhalanso m’thupi la munthu mwa mngelo wake Mtumiki, William Marrion Branham, akuitana Mkwatibwi Wake kwa Iyemwini.

Mulungu anaika mngelo Wake padziko lapansi kuti adziimire ngati kazembe Wake woyikidwa kuti alowe mu zinthu zazikulu zosadziwika zauzimu. Amazindikira ndi kutulutsa zinthu zomwe malingaliro achithupi sangazindikire. Anatumizidwa kuti abweretse chinsinsi cha Mulungu ndi kulosera zinthu zomwe zilipo, ndi zomwe zakhalapo, ndi zomwe zidzakhalapo. Iye ndi Liwu la Mulungu kwa Mkwatibwi.

Ndi chiyani chimenecho? Mulungu, Mulungu kuseri kwa zikopa, chikopa cha munthu. Kulondola kwenikweni.

Otsutsa ambiri masiku ano sangatimvetse ife okhulupirira enieni. Kwa iwo, takhala ngati nati. Amati ndife okhulupirira milungu ndipo timalambira mneneri…

Wotsutsa, masiku pang’ono apitawo, ananena kwa ine, uko mu Tucson. Iye anati, “Inu mukudziwa, anthu ena amakupangani inu kukhala nati, ndipo ena amakupangani inu kukhala mulungu.”

Ine ndinati, “Chabwino, zimenezo zimayenda bwino.” Ine ndinadziwa kuti iye amayesera kuti anditsutse ine. Mukuona?
Iye anati, “Anthu amaganiza kuti inu ndi mulungu.”

Monga momwe zinalili pamene Yesu anali padziko lapansi, ndi chimodzimodzi lero ndi mneneri Wake. Anthu sali kuseri kwa chophimba; achita khungu ku choonadi. Sitikufuna china chilichonse koma njira yoperekedwa ndi Mulungu lero: Iye mwini wophimbidwa mu thupi, Mawu a Mulungu omwe adalembedwa ndikusungidwa kwa Mkwatibwi.

Pamene Mulungu adawonekera padziko lapansi, Iye anali kubisala kuseri kwa chophimba; kuseri kwa khungu la Munthu wotchedwa Yesu. Anaphimbidwa ndikubisala kuseri kwa khungu la munthu wotchedwa Mose, ndipo iwo anali milungu, osati Milungu; koma iwo anali Mulungu, Mulungu mmodzi, akungosintha chigoba Chake, akuchita zomwezo nthawi iliyonse, kubweretsa Mawu awa. Mulungu adapanga mwanjira imeneyo.

Tangolumikizidwa ku Mawu, Uthenga wa nthawi ino. Tsopano watipanga Mawu ophimbidwa kuseri kwa thupi la munthu. Mkwatibwi ndi Mkwati ndi amodzi. Mulungu ndi mmodzi, ndipo Mawu ndi Mulungu! Talumikizidwa ndi Mawu.

Mwachisoni, kusiyana pakati pa okhulupirira lero ndikuti amamva kuti timayika kwambiri pa mneneri wotsimikiziridwa wa Mulungu. M’malo mwake, akufuna kuyika utsogoleri umenewo kwa abusa awo.

Mulungu sasintha pulogalamu Yake; amatumiza MUNTHU MMODZI kuti atsogolere Mkwatibwi Wake. Ndi Mzimu Wake Woyera mwa aliyense wa ife, kutitsogolera ndi LAWI LA MOTO.

Mawu amadza kwa mmodzi. Mu m’badwo uliwonse, chimodzimodzi, ngakhale mu mibadwo ya mpingo, kuyambira kwa woyamba womwe mpaka kwa wotsiriza. Enawo ali ndi malo awo awo, izo nzoona, zindikirani, koma muzikhala kutali ndi Lawi la Moto ilo. Mukuona?

KOMA TIKUMVA CHIYANI LERO…CHINTHU CHOMWECHO.

Inu mukukumbukira zimene Datani ndi iwo ananena uko? Iwo anati, “Tsopano, Mose, dikira apa miniti chabe! Iwe ukudzitengera wekha kwambiri, mwaona. Tsopano, aliponso anthu ena pano omwe Mulungu wawaitana.”

Sitikutsutsana ndi utumiki; Mulungu wawaitana, koma abale ndi alongo, ngati m’busa wanu sakuika Mawu a Mulungu ngati Mawu ofunikira kwambiri omwe muyenera kumva posewera matepi mu mpingo wanu, sakukutsogolerani ku njira yoperekedwa ndi Mulungu.

Izo ndi zoona. Iwo, mmodzi aliyense, amatsatira mwabwino nthawizonse pamene iwo anali kutsatira, koma pamene wina anayesera kuti adzikweze ndi kutenga malo a Mulungu amene Iye anamupatsa Mose, yemwe anali wokonzedweratu ndi wodzozedweratu ku ntchito imeneyo, kuyesera kuti aitenge iyo, moto unatsika pansi ndipo unadzatsegula nthaka ndi kuwamezera iwo mmenemo. Mukuona? Mukuona? Muzisamala. Mukuona?

Tonsefe tiyenera kulumikizidwa ku Mawu amene analankhulidwa ndi kuikidwa pa matepi. Umenewo ndiye Mtheradi wa Mulungu. Ndiwo Mawu okhawo omwe Mkwatibwi angagwirizane nawo. Utumiki sudzagwirizanitsa Mkwatibwi, koma Mawu a Mulungu okha pa matepi.

Ine sindingachite kalikonse popanda inu; inu simungachite kalikonse popanda ine; komanso sitingachite kalikonse popanda Mulungu. Kotero, pamodzi timapanga thunthu, chilumikizocho. Mulungu ananditumiza ine pa cholinga; inu mukakhulupirira izo, ndipo apo izo zizichitika. Basi ndi zimenezo, Mwaona, kutsimikiziridwa mwangwiro.

Pokhapokha pamodzi zimapanga CHIMODZI, kulumikizana. Mulungu anatumiza William Marrion Branham pa cholinga chimenecho. Ndiye, Pokhapokha ngati mukhulupirira, kodi chidzachitika; zatsimikiziridwa bwino.

Sindine amene ndikunena zimenezo, abale ndi alongo. NDI MULUNGU AKUNENA ZIMENEZO KUDZELA MWA MNENERI WAKE. Musalole munthu aliyense kukuuzani zosiyana kapena kuyesa kukufotokozerani mosiyana. LIWU LA MULUNGU LOKHA PA MATEPI NDILOMWE LINGAGWIRIZANITSE NDI KUMUFIKITSA MKWATIBWI KU UNGWIRO. NDI NJIRA INA ILIYONSE, INU SIMUDZAKHALA MKWATIBWI.

Kotero ine ndikuganiza kuti akuluakulu onse a ife timaganiza chinthu chomwe chomwecho. Mulungu, wokhala ndi khungu pa Iye! [Malo osajambulidwa pa tepi—Mkonzi.] Mulungu, wokhala ndi khungu pa Iye! Izo zikhoza kumveka ngati nati, kwa dziko, koma iyo ikukokera anthu onse kwa Iye.

Kodi mwamva zomwe wangonena kumene? Mulungu wokhala ndi khungu akukoka anthu onse kwa Iye.

Pamene dziko lapansi likulumikizidwa ndi nati, ife tikulumikizidwa ndi Liwu la Mulungu ndipo timatchedwa Mkwatibwi. Likutikoka kuti tituluke mu chisokonezochi, kupita ku Kukhalapo kwa Mulungu. Ife ndife nati ya Mawu a Mulungu.

Bwerani mudzalumikizidwe ndi Mawu a Mulungu limodzi nafe Lamlungu lino nthawi ya 12:00 P.M., nthawi ya ku Jeffersonville, pamene ilo likukokela anthu onse kwa Iye.

M’bale Joseph Branham

Uthenga: chosamvetseka. 64-0614E

Malemba: 1 Akorinto 1:18-25. / 2 Akorinto 12:11

25-1102 Kuvundukulidwa Kwa Mulungu

Uthenga: 64-0614M Kuvundukulidwa Kwa Mulungu

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mawu Opangidwa Kuwonetseredwa,

Kodi tingaganizire za Iwo! Lawi la Moto lomwelo lomwe linabwera pa anthu omwe analemba Baibulo ndi Lawi la Moto lomwelo lomwe tikulimva tsiku lililonse, kutanthauzira zinsinsi zonse za Baibulo kwa ife: Mawu a Mulungu Opangidwa kuwonetseredwa!

Mulungu anadziphimba Yekha mwa aneneri Ake akale kuti alankhule Mawu Ake kwa iwo. Ndicho chimene Iye anachita panthawiyo. Koma mumtsiku lathu lino, mneneri wathu, William Marrion Branham anali Mawu amoyo kwa anthu, ophimbidwa ndi Lawi la Moto.

Kudzozako ndi munthu. Mawu akuti Khristu amatanthauza wodzozedwayo, mwaona, “wodzozedwayo.” Ndiye, Mose anali Khristu mu masiku ake, iye anali wodzozedwayo. Yeremiya anali Khristu mu masiku ake, ali ndi gawo la Mawu a tsiku limenelo.

Mulungu amatanthauzira Mawu Ake Omwe. M’bale Branham anawalankhula; Mulungu anawamasulira. Iye anali ndi Mawu. Osati gulu, William Marrion Branham! Mulungu anapeza MUNTHU MMODZI. Sangathe kupeza malingaliro awiri kapena atatu osiyana ndi malingaliro osiyana. Iye akutenga MUNTHU MMODZI, ndipo anakhala Mawu amoyo a Mulungu ophimbidwa kuseri kwa thupi la munthu.

Sitili kuseri kwa chophimba chimenecho, ana aang’ono. Mulungu waonekera bwino kwa inu. Chophimba chakale chachipembedzo ndi chachikhalidwe chang’ambidwa ku Mawu a Mulungu, kuti chiwonekere! Mu tsiku lomaliza lino, chophimba chachikhalidwecho chang’ambidwa, ndipo apa pali Lawi la Moto. Apa Iye ali, akuwonetsa Mawu a tsiku lino. Chophimbacho chang’ambika.

Mudzawawone matepi amenewo pamene iwo azibwera, mudzaiwone imodzi iliyonse, momwe Iwo akubwerera momveka ndi momveka; ngati inu muli ndi makutu omvera, mwaona, maso openyera.

Ndicho chimene chikuchititsabe khungu anthu lero. Amafuna kunena kuti amakhulupirira kuti mneneri wa Mulungu ndiye anabweretsa Mawu, koma tsopano kudzoza kumeneko kuli pa ena kuti atitsogolere, osati mneneri.

Mneneri anatiuza kuti Mulungu sangaswe Mawu Ake. M’masiku otsiriza, ziyenera kukhala chimodzimodzi kachiwiri. Mulungu sangasinthe njira Yake, kapena kusintha Mawu Ake. Iye anati Sanasinthe. Iye nthawi zonse wakhala akutumiza aneneri Ake osati kuti abweretse Mawu Ake okha, komanso kuti atsogolere Mkwatibwi Wake.

Monga izo zimachitikira mu m’badwo uliwonse, Umulungu kuphimbidwa mu mnofu wa munthu. Zindikirani, Iye anatero. Aneneri anali Umulungu, utaphimbidwa. Iwo amakhala Mawu a Mulungu (ndi kulondola uko?) ataphimbidwa mu mnofu wa munthu. Kotero, iwo sanamuzindikire Mose wathu chonchobe, mwaona, Yesu.

Tsopano si Mawu olembedwa kwa ife okha, ndi zenizeni. Tili mwa Iye. Tsopano tikusangalala. Tsopano tikumuona Iye. Tsopano tikumuona Iye, Mawu, akudziwonetsera Yekha.

Kenako, timakhala gawo la Iye. Ndife chophimba chomwe chimamuphimba Iye. Ndife gawo la Iye; bola Khristu ali mwa inu, monga Khristu anali wa Mulungu.

Tikumanga kachisi wa Khristu kuseri kwa chophimba cha khungu lathu la munthu. Ndife makalata olembedwa, Mawu olembedwa. Ndife Mawu omwe alembedwa, owonetsedwa.

Ndipo pamene inu muwawona Mawu akuwonetseredwa, inu mwawawona Atate, Mulungu, chifukwa Mawu ndi Atate. Mawu ndi Mulungu. Ndipo Mawu, akamawonetseredwa, ndi Mulungu Mwiniwake akutenga Mawu Ake Omwe ndi kumawawonetsera Iwo pakati pa okhulupirira. Palibe kanthu kamene kangawapange Iwo kukhala amoyo koma okhulupirira, okhulupirira basi.

Mulungu, wophimbidwa mu thupi la munthu, akulankhula ndi kuwulula Mawu Ake kwa ife tsiku ndi tsiku. Mulungu mu thupi la munthu akukhala mwa aliyense wa ife.

M’bale Joseph Branham

Uthenga: 64-0614M – “Kuvundukulidwa Kwa Mulungu “
Nthawi: 12:00 P.M. Nthawi ya ku Jeffersonville

Kumbukirani kusunga nthawi ya masana

25-1026 Yang’anani Kutali Kwa Yesu

Uthenga: 63-1229E Yang’anani Kutali Kwa Yesu

PDF

BranhamTabernacle.org

Okondedwa Iwo Omvera Matepi,

Nthawi yafika yoti aliyense adzifunse kuti: “Ndikamamvetsera matepi, ndi Liwu lotani limene ndimamva? Kodi basi ndi Liwu la William Marrion Branham, kapena ndimamva Liwu la Mulungu la tsiku lathu? Kodi ndi liwu la munthu, kapena ndikumva Pakuti Atero Ambuye ? Kodi ndikufunika wina womasulira zomwe ndikumva, kapena kodi Mawu a Mulungu safunikira kutanthauzira?”

Yankho lathu ndi ili: Ife tikumva Mawu Olankhulidwa osandulika thupi. Tikumva Alefa ndi Omega. Tikumva Iye, Lawi la Moto, akulankhula kudzera m’milomo ya munthu monga momwe Iye ananenera kuti adzachitira m’masiku athu.

Sitimva munthu, timamva Mulungu, yemweyo dzulo, lero, ndi kwa nthawi zonse. Mawu a Mulungu omwe ndi achangu, amphamvu kuposa lupanga lakuthwa konsekonse, odula ngakhale fupa, ndi ozindikira malingaliro omwe ali mumtima.

Izo zavumbulutsidwa kwa ife kuti chimene Iye anali pamene ankayenda mu Galileya ndi chomwechi chimene Iye ali usikuuno ku Jeffersonville; chinthu chomwecho chimene Iye ali ku Branham Tabernacle. Ndi Mawu a Mulungu akuonekera. Chimene Iye anali panthawiyo, Iye ali usikuuno, ndipo adzakhalapo kwa nthawi zonse. Chimene Iye anati adzachita, Iye wachita.

Munthuyo si Mulungu, koma Mulungu akadali ndi moyo ndipo akulankhula ndi Mkwatibwi Wake kudzera mwa munthuyo. Sitiyenera kulambira munthuyo, koma kulambira Mulungu mwa munthuyo; pakuti iye ndi munthu amene Mulungu anasankha Iye kukhala LIWU LAKE ndikutsogolera Mkwatibwi Wake m’masiku otsiriza ano.

Chifukwa Iye watipatsa bvumbulutso lalikulu la nthawi yotsiriza, tsopano tikhoza kuzindikira YEMWE IFE TILI, Mawu osandulika kukhala thupi m’masiku athu ano. Satana sangatinyengenso, chifukwa ife tikudziwa kuti ndife namwali wake obwezeretsedwa mwathunthu, Mkwatibwi wa Mawu.

Liwu limenelo linatiuza kuti: Zonse zomwe ife tinkazisowa zapatsidwa kale kwa ife. Palibe chifukwa chodikira. Ilo lalankhulidwa, NDI LATHU, NDI LA IFE. Satana alibe mphamvu pa ife; wagonjetsedwa.

Inde, Satana akhoza kutibweretsera matenda, kuvutika maganizo, ndi chisoni, koma Atate watipatsa kale mphamvu yoti timutulutsire kunja…IFE TIMANGOLANKHULA KOKHA MAWU, Ndipo iye ayenera kutichokera….osati chifukwa chakuti ife tanena choncho, koma chifukwa chakuti MULUNGU ANANENA CHONCHO.

Mulungu yemweyo amene analenga agologolo, pamene panalibe agologolo. Zimenezo zinamupatsa Mlongo Hattie chofuna cha mtima wake: ana ake aamuna awiri. Amene anachiritsa Mlongo Branham chotupa dzanja la dokotala lisanamukhudze. Iye ndi MULUNGU YEMWEYO amene sali ndi ife kokha, KOMASO IYE ALI NDI MOYO NDIPO AKUKHALA MWA IFE. IFE NDIFE MAWU OSANDULIKA KUKHALA THUPI.

Tikamaona ndi kumvetsera Mawu pa matepi, timaona ndi kumva Mulungu akudziulula Yekha mu thupi la munthu. Timaona ndi kumva amene Mulungu anatuma kuti atitsogolere ku Dziko Lolonjezedwa. Timadziwa kuti Mkwatibwi yekha ndiye adzakhala ndi bvumbulutso limenero, motero takhala opanda mantha. Palibe chifukwa chokhala ndi manjenje, kuvutika maganizo, kukhumudwa, kudabwa kapena kuda nkhawa…NDIFE MKWATIBWI.

Mvetserani ndi kukhala ndi moyo, m’bale wanga, khalani ndi moyo!
Mvetserani Yesu tsopano ndi kukhala ndi moyo;
Pakuti zajambulidwa pa matepi, aleluya!
Ndi kuti timvetsere ndikukhala ndi moyo.

O, Mkwatibwi wa Yesu Khristu, ndi tsiku lalikulu bwanji lomwe tikukhalamo. Zimene tikuyembekezera, mphindi ndi mphindi. Tsiku lililonse tsopano tidzawona okondedwa athu, ndiye, mu mphindi ya kuthwanima kwa diso, tidzachoka pano ndipo tidzakhala nawo mbali ina. Zili moyandikira kwambiri kotero kuti zikuwoneka kuti tingazikhudze izo…ULEMERERO!

Bwerani Mkwatibwi, tiyeni tisonkhanenso mozungulira Mawu a Mulungu Lamlungu lino nthawi ya 12:00 PM, nthawi ya ku Jeffersonville, pamene Ife tikumumva Iye akulankhula nafe Mawu a Moyo Wamuyaya.

M’bale. Joseph Branham

Uthenga: 63-1229E Yang’anani Kutali Kwa Yesu

Malemba Opatulika:
Numeri 21:5-19
Yesaya 45:22
Zekariya 12:10
Yohane Woyera 14:12

25-1019 Pali Munthu Pano Yemwe Akhoza Kuyatsa Kuwala

Uthenga: 63-1229M Pali Munthu Pano Yemwe Akhoza Kuyatsa Kuwala

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mkwatibwi wa Khristu, tiyeni ife tibwere palimodzi Lamlungu 12:00 P.M., nthawi ya ku Jeffersonville, kuti tidzamve 63-1229M Pali Munthu Pano Amene Akhoza Kuyatsa Kuwala.

M’bale. Joseph Branham

25-1012 Kusimidwa

Uthenga: 63-0901E Kusimidwa

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mkwatibwi wa Tepi,

Tsopano inu anthu mu matepi kumeneko.

Ambuye, ife tingayambe bwanji kufotokoza chimene mawu aang’ono asanu ndi limodzi awa akutanthauza kwa ife, Mkwatibwi wa Yesu Khristu? Ndi Vumbulutso la Uthenga wa orali kwa ife. Ndi Mulungu akuyankhula kupyolera mwa m’thenga Wake wa mngelo kumuuza Mkwatibwi Wake, “Ine ndikudziwa inu mudzakhala ndi Liwu Langa. Ine ndikudziwa chimene Mawu Anga pa matepi awa ati adzatanthauze kwa inu.Ine ndikudziwa inu mudzakhala ndi Vumbulutso kuti Mauthenga awa amene ine ndawayankhula mu matepi ali Chizindikiro Changa cha lero.”

“Ine ndaika Liwu Langa pa matepi a maginito awa; pakuti Mauthenga awa ayenera kutsirizitsa Mawu onse. Padzakhala zikwi kuchulukitsa zikwi amene ati adzamve Liwu Langa pa matepi ndipo adzakhala ndi Vumbulutso kuti uwu ndi utumiki Wanga.Ndi mzimu woyera wa lero. Ndi uthenga wanga wa chizindikiro

“Ine ndatumiza atumiki okhulupirika ambiri ku dziko lonse lapansi kuti akalengeze utumiki Wanga. Pamene iwo anabwerera, iwo anandiuza Ine, ‘Ife tamvera malamulo Anu mwa kusewera matepi Anu.Ife tinapeza anthu amene amakhulupirira Mawu aliwonse. Iwo apanga nyumba za Iwo eni kukhala tchalitchi zolandiliramo Uthenga Wanu. Ife tinawauza iwo, onse amene akanadzabwera pansi pa Chizindikiro Chanu, Uthenga wa orali, akanadzapulumutsidwa.’”

Ndi nthawi yomwe munthu aliyense ayenera kudzifufuza ndikudzifunsa yekha, kodi njira yangwiro ya Mulungu lero ino ndi iti? Mawu a mneneri sanalepherepo nthawi imodzi. Icho chatsimikiziridwa kuti ndi Choonadi CHOKHA, CHINTHU CHOKHAKO chimene chiti chidzamuyanjanitse Mkwatibwi Wake.

Chirichonse chimene iye ananena chachitika ndendende basi momwe iye ananenera icho. Lawi la Moto likadali pano ndi ife.Liwu la Mulungu akuyankhulabe ndi ife pa matepi. Mneneri anangotiuza ife kuti Mulungu analambala pamwamba kokha pamene Iye adawona Chizindikiro. Ndi nthawi ya kusimidwa kuti onse alowe pansi pa Uthenga wa Chizindikiro uwo.

Ife taliwona Dzanja lamphavu la Mulungu mu nthawi yotsiriza ino. Iye watipatsa ife Vumbulutso loona la Mawu Ake ndipo ilo labwera pansi pa chisonyezo cha Chizindikiro. Tsopano, pamene ife tiri pansi pa chisonyezo cha Chizindikiro, tiyeni ife tibwere palimodzi ndi kudya Mgonero mwa kusimidwa; pakuti tidziwa kuti Mulungu akukozekera kuti akanthe ndi chiweruzo.

Ndikufuna kuitana aliyense wa inu kuti mumve ndi kukhala ndi M’gonero ndi Utumiki wosambitsana Mapazi Lamlungu lino, pamene tikumva Uthenga: Kusimidwa 63-0901E.

Uthenga ndi utumiki wa Mgonero udzakhala pa Wailesi Ya Liwu kuyambira 5:00 P.M. nthawi ya ku Jeffersonville . Chonde khalani omasuka kukhala ndi chiyanjano chanu nthawi ya kwanuko ngati mungafune, monga ndikudziwira kuti zidzapangitsa kukhala kovuta kwa okhulupirira athu ambiri akunja kuyamba chiyanjano chawo panthawiyo. Padzakhala ulalo wa fayilo yotsitsika ya utumiki.

M’bale. Joseph Branham

Malemba oti muwerenge musanayambe chiyanjano:

Ekisodo 12:11
Yeremiya 29:10-14
Luka 16:16 St
Yohane 14:23
Agalatiya 5:6
Yakobo 5:16

25-1005 Chizindikiro

Uthenga: 63-0901M Chizindikiro

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mkwatibwi Wa Chizindikiro

Pamene ife tibwera palimodzi, ife sitimangoyankhula za Uthenga, ife timabwera palimodzi kuti tidzaike Magazi, kuti tiike Chizindikiro; ndipo Chizindikiro ndi Uthenga wa orali! Ndiwo Uthenga wa tsiku lino! Ndiwo Uthenga wa nthawi ino.

Ife tayika Chizindikiro icho kwa ife eni, ku nyumba zathu, ndi kwa mabanja athu. Sitikuchita manyazi. Sitisamala amene akudziwa. Tikufuna kuti aliyense adziwe, wodutsa aliyense awone ndi kudziwa: Ndife Anthu a atepi. Ndife a Tepi yapa nyumba . Ndife Mkwatibwi wa Tepi wa Mulungu.

Mzimu Woyera = Chizindikiro = Uthenga. Onse ali ofanana. Simungathe kuwalekanitsa. Atate, Mwana, Mzimu Woyera = Ambuye Yesu Khristu. Simungathe kuwalekanitsa. Uthenga = Mtumiki. Ziribe kanthu zomwe otsutsa anena, M’NENERI ANATI, inu simungakhoze kuwalekanitsa iwo.

Mulungu ndiye chimwemwe chanu. Mulungu ndiye mphamvu yanu. Kudziwa Uthenga uwu, kudziwa kuti Iwo ndi Choonadi chokha, kudziwa kuti Icho ndi Chizindikiro, ndiko kukwanira kwathu. Ena akhoza kunena, “Ine ndimawakhulupirira Iwo, ine ndimawakhulupirira Iwo, ine ndikukhulupirira Iwo ndi Choonadi. Izo zonse nzabwino, komabe Izo ziyenera kuyikidwa.

Mneneri anati Uthenga uwu ndi Chizindikiro cha lero. Uthenga uwu ndi Mzimu Woyera. Ngati inu muli ndi Vumbulutso lirilonse la Uthenga uwu inu mukhoza kuwona momveka ora limene ife tikukhalamoli. Ochuluka kwambiri akunena, “Ine ndikukhulupirira Iwo. Mulungu anatumiza mneneri. Iwo uli Uthenga wa ora,” koma Iwo amadzitama ponena kuti iwo satero, ndipo sadzatero, kusewera Liwu lomwe la Chizindikiro mu mipingo yawo.

Mulungu sanalankhule kupyolera mwa mngelo Wake wamphamvu ndi kungonena chinachake pokhapokha ngati chinali ndi tanthauzo. Iye anatiuza ife kuti anatiphunzitsa ife mwa zoimira ndi mithunzi. Mu Uthenga uwu, mneneriyu akufotokoza mwatsatanetsatane kutiuza zimene Rahabi ndi a banja lake anachita kuti apulumutsidwe, kuti akhale Mkwatibwi. Anafotoza momveka bwino pa zomwe mkaziyo anachita.

Pamene anyamata a tepi ankasewera “TEPI”…Dikirani miniti, kodi mthenga uja anachita chiyani? Anasewera Tepi. Ndiye kodi iye anachita chiyani? Anayipanga iye nyumba yake MPINGO WA TEPI. Iye sanachite manyazi kunena kuti, “Onani chingwe chofiyira icho, izo zikutanthauza kuti ine ndine wa MPINGO WA TEPI”.

Inu mukuganiza ngati iye akanati, “Inde, ine ndikumukhulupirira m’thenga ndi Uthenga, koma ife sitimaseweranso Matepi ndipang’ono pomwe mu mpingo wathu. Ndili ndi m’busa amene amati AYI, iyeyo ayenera kungolalikira ndi kubwereza zomwe matepi amanena.” Inu mukuganiza kuti mkazi uja akanapulumutsidwa…???

Iye anaika chizindikiro, ndipo nyumba yake inapulumutsidwa, kapena iye akanawonongeka kumusi uko komwe iye anali.

Mwamvapo atumiki ambiri akupereka zifukwa zodzikhululukira ponena za kusewera matepiwo, koma ambiri a iwo amati: “Mneneri sananenepo kuti azisewera matepiwo m’tchalitchi.”

Mneneri anati Rahabu anayipanga iye nyumba yake kukhala tchalitchi, ndipo mpingo wake unkasewera Matepiwo. Ndipo chifukwa chakuti iye ankasewera Matepi mu mpingo wake, iye, ndi Mpingo wake wonse wa TEPI, anali pansi pa Chizindikiro ndipo anapulumutsidwa. Mpingo wina uliwonse unawonongeka.

Abale ndi alongo, chonde, ine sindikunena kuti m’busa sangakhoze kulalikira Uthenga uwu, kapena kuti ndi zolakwika ngati iye atero. Mwa njira yanga yanga, Ine ndikulalikira tsopano kupyolera mu kalata iyi, koma tsegulani mtima wanu ndi kumvetsera zimene mneneri akunena ndi kukuchenjezani inu. Ngati m’busa wanu akukana, kapena adzakana, kuti azisewera matepi mu mpingo wanu pakupanga chowiringula cha mtundu wina; chirichonse chimene chingakhoze kukhala ziribe kanthu kuchuluka kwa zomwe iye anena “Ine ndikukhulupirira Uthenga wa orali,” molingana ndi zomwe ine ndikukhulupirira Mawu akunena, Chizindikiro, Uthenga wa orali, iwo sukuyikidwa.

Lamlungu lino, ine ndikukuitanani inu kuti mubwere mudzamvetsere ndi Branham Tabernacle pa 12:00 p.M., nthawi ya ku Jeffersonville, ku Uthenga: Chizindikiro 63-0901M. Ngati inu simungakhoze kutijowina ife, sewerani Uthenga wa Chizindikiro uliwonse, ndi kuwuyika Iwo.

M’bale. Joseph Branham

Malemba oti muwerenge musanamve Uthenga:

Genesis 4:10
Ekisodo chaputala 12
Yoswa mutu 12
Machitidwe 16:31/19:1-7
Aroma 8:1
1 Akorinto 12:13
Aefeso 2:12/4:30
Ahebri 6:4 / 9:11-14 / 10:26-29 / 11:37 / 12:24 / 13:8, 10-20
Yohane 14:12

25-0928 Nthawi Yolumikizana Ndinso Chizindikiro

Uthenga: 63-0818 Nthawi Yolumikizana Ndinso Chizindikiro

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mkwatibwi Wolumikizitsidwa,

Ndine wokondwa kwambiri, ndipo pansi pa chiyembekezero chachikulu chotero, kukhala gawo la zonse zomwe Mulungu akuchita mu tsiku lathu. Malingaliro a Mulungu pachiyambi tsopano akukwaniritsidwa pamaso pathu, ndipo ife ndife gawo la icho.

M’Baibulo lonse, aneneri analosera ndi kunena zimene zikanadzachitika. Nthawizina mauneneri amenewo sanakwaniritsidwe kwa mazana a zaka kenako, koma pamene chidzalo cha nthawi chinadza, icho chinafika pochitika; pakuti ganizo la Mulungu loyankhulidwa mwa mneneri wake liyenera kuchitika.

Mneneri Yesaya anati, “namwali adzaima.” Banja lililonse la Aheberi linakonzekeretsa mwana wawo wamkazi kuti abereke mwana. Iwo anagula izo nsapato ndi nsapato, ndi Birdseye wamng’ono, ndipo anakonzekera kuti mwanayo abwere. Mibadwo inapita, koma potsiriza Mawu a Mulungu anakwaniritsidwa.

Monga kamnyamata ine kakukula nthawizonse ndimadabwa, Ambuye, ine ndikuwona mu Mau anu kuti nthawi zonse mumagwirizanitsa anthu anu pamodzi kuti akwaniritse mawu anu. Munagwirizanitsa ana Anu Achihebri pamodzi mwa munthu mmodzi, Mose, amene anawatsogolera iwo ndi Lawi la Moto kupita ku Dziko Lolonjezedwa.

Pamene Inu munakhala thupi ndi kukhala pa dziko lapansi, Inu munagwirizanitsa ophunzira Anu. Inu munawalekanitsa iwo ku chirichonse ndi aliyense kuti awulule Mawu Anu kwa iwo. Pa tsiku la Pentekosite, munasonkhanitsanso Mpingo Wanu palimodzi pa malo amodzi, mu malingaliro amodzi ndi mtima umodzi musanabwere ndi kuwapatsa iwo Mzimu Woyera.

Ndinaganiza, zingatheke bwanji lero Ambuye? Mkwatibwi wanu wamwazikana padziko lonse lapansi. Kodi Mkwatibwi yense adzabwera ku Jeffersonville? Sindikuwona zomwe zikuchitika Ambuye. Koma Ambuye, Inu simumasintha dongosolo Lanu. Ndi Lamulo Lanu, palibe njira yoletsera. Inu muzichita motani izo?

ULEMERERO…LERO, tikhoza kuona ndi maso athu, ndipo koposa zonse, KHALANI GAWO LA ICHO: Mawu Amuyaya a Mulungu akukwaniritsidwa. Sitili MWATHUPI pamalo amodzi, tafalikira padziko lonse lapansi, koma Mzimu Woyera TSOPANO WALUMIKIZANITSA MKWATIBWI WAKE NDI MAWU A MULUNGU. MAWU AKE ANALANKHULIDWA NDIPO ANAJAMBULIDWA PA MATEPI, Mtheradi wa Mulungu wa lero, ukusonkhanitsa ndi KULUMIKIZANITSA MKWATIBWI WAKE… NDIPO PALIBE CHINACHILICHONSE CHINGAYIMITSE ICHO.

Mulungu akulumikizitsa Mkwatibwi Wake. Iye akubwera pamodzi, kuchokera Kummawa ndi Kumadzulo, ndi Kumpoto ndi Kummwera. Pali nthawi yolumikizana, ndipo iyo ikuchitika pakali pano. Kodi Iye akulumikizanira chiyani? Mkwatulo. Amen!

Nthawi yolumikizana ikuchitika PANO!!! Kodi chikutigwirizanitsa ndi chiyani? Mzimu Woyera mwa Mawu Ake, Liwu Lake. Kodi tikugwirizanitsa chiyani? MKWATULO!!! Ndipo tonse tikupita ndipo sitikusiya MMODZI kumbuyo.

Mulungu akumukonzekeretsa Iye. Inde bwana, kulumikizana! Kodi Iye akulumikizana ndi chiyani? Ndi Mawu!

Kodi Mawu amasiku ano ndi chiyani? UTHENGA uwu, MAWU AKE, Liwu la Mulungu kwa Mkwatibwi Wake. Osati mwamuna. Osati amuna. Osati gulu. Otsimikiziridwa, ndi Lawi la Moto, MAWU a Mulungu pa matepi.

“Pakuti miyamba yonse ndi dziko lapansi zidzapita, koma Mawu Anga sadzapita.” Iye akudzilumikizitsa Iyemwini ndi PAKUTI ATERO AMBUYE mosalabadila zimene chipembedzo chirichonse kapena wina aliyenseyo akunena.

Mosasamala chimene ALIYENSE anena, ife tikulumikizana ndi zotsimikiziridwa, zotsimikiziridwa, Atero Liwu la Ambuye la tsiku lathu. Osati kutanthauzira kwa wina; tingachite bwanji zimenezo? Izo zimasintha ndi munthu aliyense, koma Liwu la Mulungu pa matepi SALISINTHA ndipo Ilo lalengezedwa ndi Lawi la Moto Lokha kuti ndi Mawu a Mulungu ndi Liwu la Mulungu.

Vuto lake ndi lakuti, ndi munthu, iye samamudziwa mtsogoleri wake. Inde, bwana. Iwo amasonkhanira chipembedzo, iwo amamusonkhanira bishopu kapena munthu, koma iwo sangamusonkhanire Mtsogoleri, Mzimu Woyera mu Mawu. Mukuona? Iwo amati, “O, chabwino, ine ndikuwopa ine ndikhala wotengeka pang’ono; ine ndikuwopa ine ndiponda phazi lolakwika.” Ohhhh, ndi zimenezotu!

Apa ndi pamene otsutsa amalozera kwa mipingo yawo ndi kuti, “Onani, iwo akukwezera mmwamba munthu, M’bale Branham.

Zachabechabe, tikulumikizana mozungulira MAWU OYENZEDWA A MULUNGU OLANKHULIDWA KUPYOLERA MUNTHU UYO. Kumbukirani, ameneyo ndi mwamuna yemwe Mulungu anamusankha kuti akhale Liwu Lake kuti aitane ndi kutsogolera Mkwatibwi Wake mu tsiku lino. Limenelo ndi Liwu LOKHALA lotsimikiziridwa ndi Mulungu Mwiniwake.

Koma mophonya , IWO akulumikizana mozungulira ANTHU. Iwo sakusewera Liwu la Mulungu pa matepi mu mipingo yawo. Kodi inu mungaganize moteromo??? Mtumiki amene amadzinenera kuti akukhulupirira Uthenga uwu kuti ndi Uthenga wa nthawi ino, pakuti Atero Ambuye, koma akupeza chowiringula chamtundu wina choti SANGAKHOZE kusewera Liwu limenelo mu mipingo yawo, koma azitumikira kwa anthu iwo AYENERA kumvetsera kwa iwo ndi atumiki ena akulalikira Mawu… ndiye amati ife tikutsatira munthu!!!

Tangomva Lamulungu lapitali zomwe Mulungu anawachitira amuna amenewo!!

Tikukonzekera Ukwati. Ife tikukhala Mmodzi ndi Iye. Mawu amakhala inu, ndipo inu mumakhala Mawu. Yesu anati, “Pa tsiku limenelo inu mudzadziwa izo. Onse Atate ali, Ine ndine; ndipo zonse Ine ndiri, inu muli; ndipo nonse inu muli, Ine ndiri. Mu tsiku limenelo inu mudzadziwa kuti Ine ndiri mwa Atate, Atate mwa Ine, Ine mwa inu, ndi inu mwa Ine.”

Zikomo Ambuye chifukwa cha Vumbulutso la Inu Nokha, ndi ifeeni, mu tsiku lathu. Mkwatibwi Wanu podzikonzekeretsa Yekha ndi Mawu Anu Olankhulidwa. Tikudziwa kuti tili mu Chifuniro Chanu changwiro pakukhala ndi Mawu Anu olembedwa.

Ndikuitana dziko kuti limvetsere ku Liwu lokhalo lotsimikiziridwa la Mulungu la tsiku lathu Lamulungu lino. Muli wolandiridwa kulumikizana nafe Lamulungu nthawi ya 12:00 p.m., nthawi ya ku Jeffersonville, pomwe tikumvera: 63-0818, Nthawi Yolumikizana Ndinso Chizindikiro . Ngati simungathe kulumikizana ndi kumvetsera nafe, sankhani tepi, TEPI ILIYONSE; iwo onse ali pakuti Atero Ambuye, ndipo mvetserani ku Mawu a Mulungu kukupangani inu kukhala angwiro ndi kukupangani inu kukonzekera kubwera Kwake posachedwa.

M’bale. Joseph Branham

Masalimo 86:1-11
Mateyu 16:1-3

Iye akudzilumikizitsa Iyemwini. Iye akukonzekera. Chifukwa chiyani? Iye ndi Mkwatibwi. Uko nkulondola. Ndipo Iye akudzilumikizitsa Iyemwini ndi Mkwati Wake, mwaona, ndipo Mkwati ndi Mawu. “Pachiyambi panali Mawu, Mawu anali ndi Mulungu, ndipo Mawu anali Mulungu. Ndipo Mawu anasandulika thupi ndipo anadzakhala pakati pathu.”

25-0921 Chitsutso

Uthenga: 63-0707M Chitsutso

PDF

BranhamTabernacle.org

Okondedwa Iwo Omasulidwa,

Tsopano, kumeneko, “iwo,” osati wochimwa. “Iwo,” amenewo ndi, mpingo wa tsiku limenelo, iwo anapeza cholakwika ndi Munthu Yemwe anali Mawu. Ndi kulondola uko? Iwo anapeza cholakwika ndi Munthu Yemwe anali Mawu. Tsopano iwo akupeza cholakwika ndi Mawu akugwira ntchito kupyolera mwa munthu.

Kuyambira pachiyambi dziko lamukana Iye, linamukana Iye, linakana kukhala ndi Mawu Ake pa kusunga ndi miyambo yawo, zikhulupiriro zawo, malingaliro awo. Iwo nthawizonse amaphonya dongosolo la Mulungu; Mulungu, monga Munthu, yemwe anali Mawu, ndipo tsopano Mawu akugwira ntchito kupyolera mwa munthu.

Koma mu tsiku lathu Iye anati, “Ine ndidzakhala nawo gulu laling’ono, osankhidwa apang’ono, iwo anali mwa Ine kuchokera pachiyambi. Iwo adzandilandila Ine ndi kudzakhulupilira mau anga ndi Munthu yemwe Ine ndinamusankha kudzaulula mau anga. Iye adzakhala Liwu Langa kwa iwo

“Iwo sadzachita manyazi kulalikira Liwu Langa.” Iwo sadzachita manyazi kuuza dziko kuti Ine ndabwera kachiwiri ndipo ndadziwonetsera Ndekha kupyolera mu thupi la munthu monga Ine ndinanenera kuti Ine ndidzachita. Nthawi imeneyi iwo sadzamupembedza munthuyo, koma iwo azidzandipembedza Ine, Mawu, amene ati adzayankhule kupyolera mwa munthu. Adzandikonda Ine ndi kundilengeza mu m’tsempha uliwonse wa umunthu wawo.”

“Potero, Ine ndawapatsa iwo zonse zomwe iwo akusowa kuti akhale Mkwatibwi Wanga. Ine ndawalimbitsa iwo ndi Mawu Anga; pakuti iwo ALI MAWU ANGA atasandulika thupi. Ngati iwo akusowa machiritso, iwo alankhule Mawu Anga. Ngati iwo ali ndi chotchinga chirichonse chimene chimawatchinga iwo, iwo alankhule Mawu Anga. Ngati iwo ali ndi mwana yemwe walowelela, iwo alankhule Mawu Anga. Chirichonse chimene iwo akusowa, iwo alankhule Mawu Anga, pakuti iwo ali Mawu Anga opangidwa thupi mwa iwo.”

“Iwo akudziwa omwe iwo ali, pakuti Ine ndadziululira Inemwini kwa iwo. Iwo akhala owona ndi okhulupirika ku Mawu Anga ndipo akulumikizana palimodzi kuzungulira Liwu Langa.Pakuti iwo akudziwa Liwu Langa, Mawu Anga, Mzimu Wanga Woyera. Iwo akudziwa, kumene kuli Mawu, Mphungu zidzasonkhanitsidwa.”

Pamene mneneri Wake akulankhula Mawu Ake ndi kuwutsutsa m’badwo uno wa kumupachika Yesu Khristu kachiwiri ndi kulengeza kuti iwo awonongedwa, Mkwatibwi adzakhala akusangalala. Pakuti ife tikudziwa IFE NDIFE Mkwatibwi Wake yemwe wawavomereza ndi kuwalandira Mawu Ake. Timafuula kuchokera pansi pamtima kuti:

Ndine Wanu, Ambuye. Ine ndikudzigoneka ndekha pa guwa ili, basi modzipatula monga ine ndikudziwira kuti ndidzipange ndekha. Tengani dziko lichoke mwa ine, Ambuye. Tengani zinthu kuchokera kwa ine zomwe ziri zakutha; ndipatseni ine zinthu zosatha, Mawu a Mulungu. Mundirole ine ndikhoze kumakhala moyo Mawu amenewo mwapafupi kwambiri, mpaka Mawu akhale ali mwa ine, ndi ine mu Mawu. Perekani izi Ambuye. Mundirole ine ndisadzachoke konse kwa Iwo.

Pali moyo, ndipo pali imfa. Pali njira yolondola, ndipo pali njira yolakwika. Pali choonadi, ndipo pali bodza. Uthenga uwu, Liwu ili, ndi njira yangwiro yoperekedwa ndi Mulungu ya lero. Bwerani mudzajowine gawo la Mkwatibwi wamphamvu wa Mulungu pamene tikusonkhana mozungulira Mawu Ake owululidwa ndi kumva Uthenga: Chitsutso 63-0707M.

M’bale. Joseph Branham

25-0914 Kodi Moyo Wanu Ndi Woyenera Uthenga?

Uthenga: 63-0630E Kodi Moyo Wanu Ndi Woyenera Uthenga?

PDF

BranhamTabernacle.org

Okondedwa Abale ndi Alongo,

Ine ndimawakonda Ambuye, Mawu a Mulungu, Uthenga uwu, Liwu Lake, mneneri Wake, Mkwatibwi Wake, kuposa moyo iwomwini. Onse ali MMODZI KWA INE. Ine sindikufuna konse kunyengerera pa cholemba chimodzi, kachidutswa kamodzi, kapena MAWU AMODZI amene Mulungu anawalemba mu Mawu Ake kapena anayankhula kupyolera mwa mneneri Wake. Kwa ine, Zonse ndi Atero Yehova.

Mulungu ankaganiza Izo, ndiye anayankhula Izo kwa aneneri Ake, ndipo iwo analemba Mawu Ake. Ndiye Iye anatumiza mngelo Wake wamphamvu, William Marrion Branham, ku dziko lapansi mu tsiku lathu kotero kuti Iye akhoze kudziulula Yekha mu thupi la munthu kamodzinso, monga Iye anachitira ndi Abrahamu. Ndiye Iye analankhula kupyolera mwa mneneri Wake kuti akhale Liwu la Mulungu kwa dziko, kuti awulule ndi kutanthauzira zinsinsi zonse zimene zabisika kuchokera ku maziko a dziko kwa Mkwatibwi Wake wokonzedweratu.

Tsopano, Mkwatibwi Wake, INU, mukukhala Mawu osandulika thupi; Mmodzi ndi Iye, Mkwatibwi Wake wa Mawu wobwezeretsedwa kwathunthu.

Ndikudziwa kuti sindikumvetsetsa zomwe ndikunena komanso zomwe ndimalemba. Ndiloleni ndinene modzichepetsa monga momwe mneneri wathu ananenera, sindine wophunzira ndipo ndikudziwa kuti sindingathe kulemba kapena kulankhula molondola zimene ndikumva mumtima mwanga. Ndikuvomereza kuti zikuwoneka ngati ndimalemba mwawukali nthawi zina. Pamene nditero, sikusonyeza kupanda ulemu, kapena kukhala ndi maganizo olakwika kapena kuweruza wina, koma mosiyana. Ndimachita izi chifukwa chokonda Mawu a Mulungu mumtima mwanga.

Ine ndikufuna kuti aliyense avomereze ndi kukhulupirira Uthenga uwu umene Mulungu anatumiza kudzayitana Mkwatibwi Wake. Sindinamvepo mumtima mwanga kapena malingaliro anga kuti atumiki sayenera kulalikiranso; zikanakhala zikutsutsana ndi Mawu a Mulungu. Ndine wachangu chabe pa Mau a Mulungu pa matepi. Ine ndikukhulupirira kuti ndilo Liwu lofunika kwambiri lomwe ATUMIKI ONSE ayenera kuyika POYAMBA pamaso pa anthu. Izi sizikutanthauza kuti sangathe kulalikira, ndikungofuna kuwalimbikitsa kuti azisewera matepi mu mipingo yawo pamene anthu asonkhana pansi pa kudzoza kumeneko.

Inde, ndikanakonda kukhala ndi dziko lonse lapansi likumvetsera Uthenga womwewo nthawi imodzi padziko lonse lapansi. Osati chifukwa “ine” ndinanena chomwecho, kapena chifukwa “Ine” ndinasankha tepi kuti ndimvetsereko, koma ine ndikumverera ndithudi Mkwatibwi akanawona momwe Mulungu wakonzera njira kuti izi zichitike mu tsiku lathu.

Ngati ife tikanakhala nazo zojambulidwa za Yesu akuyankhula lero pa tepi, osati Mateyu, Marko, Luka kapena zolemba za Yohane za zomwe Yesu ananena (pakuti iwo onse ananena izo mosiyana pang’ono), koma nkumakhoza kumva Liwu la Yesu, umunthu Wake, makutu Ake, ndi makutu athu omwe, kodi utumiki lero unganene kwa mpingo wawo, “Ife sitidzasewera zojambulidwa za Yesu kuti ndizilalikira kwa Inu ndi kudzozedwa kwa izo mu mpingo wathu. Ine ndi woyitanidwa ndi odzozedwa kuwulalikira Iwo ndikumaubwereza iwo. Inu basi muzikavetsera ku Iwo mukapita kunyumba kwanu.” Kodi anthu angakhoze kumayima ndi zimenezo? N’zomvetsa chisoni kuziyankhula kuti zimenezi ndendende n’zimene akuchita lero lino. PALIBE KUSIYANA, ziribe kanthu momwe Iwo amachipanga icho kukhala choyera.

Kwa ine, M’bale Branham anatipatsa ife chitsanzo. Iye ankakonda pamene mipingo yonse, nyumba, kapena kulikonse kumene iwo anali, anali pa kulumikizana kotero kuti iwo azitha kumva Uthenga onse nthawi imodzi. Iye ankadziwa kuti iwo akanakhoza, ndipo akanati, awatenge matepi ndi kuwamva iwo kenako, koma iye ankawafuna iwo kuti akhale olumikizana ndi kumamva Uthenga onse pa nthawi imodzi…. KWA INE UMO NDIMOMWE ANALILI MULUNGU AKUSONYEZA MKWATIBWI WAKE MOMWE ZIDZAKHALIRE MU TSIKU LATHU NDI ZOYENERA KUCHITA.

Mtumiki woona aliyense wokhulupirira Uthenga adzavomereza kuti palibe chachikulu kuposa kukhala pansi pa kudzoza kwa Liwu la Mulungu, limene linajambulidwa ndi kuikidwa pa matepi. Mkwatibwi adzakhulupirira, ndi kukhala ndi Vumbulutso, kuti Uthenga uwu ndi Mawu a Mulungu a lero. Ine ndikhoza kungoweruza ndi Mawu, koma aliyense amene sakanati Uthenga uwu uli Mtheradi wawo alibe Vumbulutso la Mawu la lero, chotero, iwo angakhoze bwanji kukhala Mkwatibwi Wake?

Sikuti kumangobwereza izo, kulalikira kapena kuziphunzitsa izo, koma kuzimva izo pa matepi ndi MALO OKHAWO omwe Mkwatibwi anganene kuti ine ndimakhulupirira Mawu aliwonse. Uthenga uwu uli PAKUTI ATERO AMBUYE. Chimene ine ndimalalikira kapena kuphunzitsa si PAKUTI ATERO AMBUYE, koma chimene Liwu la Mulungu limanena pa matepi CHILI…

Ine ndikudziwa alipo abale ndi alongo amene amati, ndi kumverera, “Ngati inu simukumvera Uthenga wa Branham Tabernacle nsanamira, kuwerenga makalata a Mphungu Zikusonkhana, ndi kumamvetsera mnyumba zanu pa nthawi yomweyo inu simuli Mkwatibwi,” kapena, “Ndi kulakwa kupita ku tchalitchi, inu muyenera kukhala mnyumba mwanu.” NDIKULAKWA KWAMBIRI. Ine sindinayambe ndaganizapo zimenezo, kunena izo, kapena kukhulupirira izo. Izo zapangitsa ngakhale kupatukana kochuluka, zomverera zolimba, ndi kuchotsedwa pakati pa Mkwatibwi ndipo mdani akugwiritsa ntchito izo kuwalekanitsa anthu.

Ine sindikufuna konse kumulekanitsa Mkwatibwi, ine ndikufuna kuti ndimulumikize Mkwatibwi monga Mawu ananenera TIYENERA KUKHALA WOLUMIKIZANA NGATI MMODZI. Ife tisamakangane wina ndi mzake, koma palibenso china mophweka chimene chingatilumikizitse ife koma Liwu la Mulungu pa matepi.

Ife Sitiyenera kumakangana ndikuuza anthu zomwe AYENERA KUCHITA kapena kuti iwo si Mkwatibwi, inuyo ingochitani monga AMBUYE AKUKUTSOGOLERANI. Iwo akali abale ndi alongo athu. Tifunika kukondana ndi kulemekezana.

Tsopano, musakangane. Mwaona? Kupsa mtima kumabweretsa mkwiyo. Chinthu choyamba inu mukudziwa, inu mukukwiyitsa Mzimu Woyera kuchoka kwa inu, inu mudzakhala mukukangana mobwezera. Ndiye Mzimu Woyera umayamba kuwuluka. Kupsa mtima kumabweretsa mkwiyo.

Ndi zimene mneneri ananena apa, ine sindikufuna konse kumvetsa chisoni Mzimu Woyera. Sindikufuna kukangana. Titha kukambirana mwachikondi, koma osati kukangana. Ngati ndalankhula chilichonse chomwe chakhumudwitsa wina aliyense mu zomwe ndalemba kapena kunena, ndikhululukireni, sichinali cholinga changa.

Monga ndanenera kale, ndikumva kuitana pa moyo wanga kuchokera kwa Ambuye kuti ndilole anthu ku Mawu a Mulungu lero. Atumiki ena ali ndi maitanidwe ena ndipo mwina amawona zinthu mosiyana. Utumiki wanga ndi kungomuuza Mkwatibwi kuti, “KUKANIKIZA KUSEWERA” ndi “Liwu la Mulungu pa matepi ndilo Liwu lofunika kwambiri limene mungamve.” “Ine ndikukhulupirira kuti utumiki uyenera kumasewera Liwu la Mulungu pa matepi mu mipingo yawo.”

Makalata amene ine ndimalemba sabata iliyonse ndi a gawo la Mkwatibwi amene amadzimva kuti ali gawo la Branham Tabernacle. Ndikudziwa kuti ena ambiri amawawerenga, koma ndili ndi udindo wochita zomwe ndikumverera kuchitidwa mu tchalitchi chathu. Mpingo uliwonse uli wa pawokha; iwo ayenera kuchita monga iwo akumverera kutsogozedwa ndi Ambuye kuti achite, ndiwo 100% Mawu. Ine Sindikutsutsana nawo iwo, timangosagwirizana. Kwa ine ndi Branham Tabernacle, ife tikungofuna kokha basi kuti tizimva Liwu la Mulungu pa matepi.

Ine Ndimaitana dziko kuti lizijowinana nafe sabata iliyonse. Ndimawalimbikitsa kuti ngati sangathe kujowinana nafe, kusankha tepi, tepi iliyonse, ndikuyikanikiza kuisewera iyo. Iwo adzadzozedwa kuposa kale. Kotero, ine ndikukuitanani inu sabata ino kuti mudzajowinane nafe Lamlungu pa 12:00 P.M., nthawi ya ku Jeffersonville, pamene ife tidzasonkhana pamodzi ndi kumva, 63-0630E Kodi Moyo Wanu Ndi Woyenera Uthenga?

M’bale Joseph Branham