Ine ndikukumbukira pomwe ndinali mnyamata wachichepere ndikukula, ndikuyesera kusankha tepi yoti ndimvere. Pamene ndinali kuwerenga mitu yomwe ndimaganiza nthawi zonse, Ine sindinkafuna kumvera Chikwati ndi Chilekano, chifukwa zimenezo zinalibe chochita ndi ine; zinali za anthu okwatira okha.
Kenako tsiku lina, pamene ndimamvetsera Chikwati ndi Chilekano, Atate anandipatsa Vumbulutso la Uthenga umenewo. Kudzoza Kwake kunabwera mumtima mwanga. Iye akulankhula nane. Uthenga uwu NDI wa ine. Iye akundiuza ine kuti Iye anandisankha ine maziko a dziko la pansi asanakhazikitsidwe. Uwu ndi mwambo wa ukwati wanga. Ine Sindikufuna wina koma Iye. Ine ndine woona mtima komanso wokhulupirika kwa Iye, ndi Mawu Ake, ndi Liwu Lake, LOKHALO. Ife ndife M’MODZI.
Zoonadi Uthenga uwu unali kwa abale ndi alongo ambiri omwe anali okwatirana ndipo tsopano analekana, ndipo Iye anali kuwauza iwo chomwe anali kuyenera kuchita; koma panali tanthauzo la patali LOKWANIRA NDI LALIKULU kwambiri, lalikulu kwambiri, lamphamvu kwambiri.
Panali Mwamuna m’modzi, ndipo Iye anali kuyitana ndi kulankhula kwa Ake ambiri, mkwatibwi wosankhidwa. LIWU LA MULUNGU LINALI KUITANA WAKE WOYERA, WOSAWONONGEDWA, NAMWALI MKWATIBWI WA MAWU. Mmodzi amene sanakhudzidwe kapena kuipitsidwa ndi munthu. Mmodzi woona mtima komanso wokhulupirika kwa Iye ndi Mawu Ake okha. Mmodzi amene anakhutitsidwa kwathunthu ndi Iye ndi Mawu Ake.
Mwa Chisomo ndi Chifundo Chake, lero tinganene, popanda mthuzi umodzi wa kukayika, IFE NDIFE NAMWALI WAKE MKWATIBWI WA MAWU. ULEMERERO!!
Iye ankafuna kutsimikiza kuti sipadzakhala malire omasuka pankhani yoitana Mkwatibwi Wake, kotero Iye anabwera yekha ndikukhala m’thupi la munthu kuti awulule Mawu Ake ndikuitana Mkwatibwi Wake kwa Iyemwini. Iye anali Elieza amene akanasankha Mkwatibwi Wa Iyemwini.
Kuti titsimikizire kuti palibe njira yoti tisokonezedwe ndi amene anali kutifunsira ukwati, Iye mwini anatsimikizira chotengera chake chosankhidwa mwa kulankhula naye kuchokera mu mphepo yamkuntho yopachikidwa pamtengo. Kenako Iye analankhula naye moonekera pa Mtsinje wa Ohio pamaso pa anthu zikwizikwi.
Iye ngakhaleso anajambulidwa chithunzi chake pamodzi ndi Iye kotero onetsani ndi kuliwuza dziko lonse lapansi , INE NDINAKUWUZANI INU KUTI INE NDIKANADZABWERANSO NDI KUDZAKHALA NDI MOYO MU THUPI. IYE NDIYE AMENE INE NDINASANKHA KUKHALAMO NDI MOYO, KUTI NDIKUITANENI INU KUTI MUKHALE MKWATIBWI WANGA. SI IYE; NDI INE NDIKULANKHULA KUDUTSIRA MWA IYE. INE NDIKUNGOGWIRITSA NTCHITO LIWU LAKE KUTI LIKHALE LIWU LANGA KWA INU. INE NDIYE AMENE NDAKUYITANANI INU KUTI MUKHALE MKWATIBWI WANGA WANGWIRO.
Vumbulutso la Uthenga Uwu, Mawu Ake, Liwu Lake, ndipo tsopano chomwe amene IFE tili ndizopitirira mawu a munthu kuti ayesere kufotokoza. Ine ndikudziwa kuti inu mukudziwa chenicheni chomwe ine ndikunena. Kukwatulidwa mu Chikhulupiriro kukuchitika. Mkwatibwi akudzikonzekeretsa yekha pokhala mu mkupezeka kwa Mulungu Mwiniwake, kukhala wangwiro.
Ndi mwayi waukulu kwambiri wotani womwe dziko lapansi lili nawo womva Liwu la Mulungu likulankhula ndi iwo; kukhala pansi ndi kumvetsera Mawu pa Mawu pamene Iye akulankhula ndi kuwulula Mawu Ake ndikutiuza amene ife tili. Palibe china choponsa kukhala mumkupezeka Kwake, choncho bwerani mudzalumikizane nafe Lamlungu nthawi ya 12:00 P.M., nthawi ya ku Jeffersonville, pamene ife tikumumva Iye akulankhula ndi Mkwatibwi Wake, Uthenga, “Chikwati Ndi Chilekano” 65-0221M.
Tsiku lija ndi Lero. Nthawi ija ndi ino. Mulungu anatumiza mphungu Yake ya mphamvu padziko lapansi kuti idzayitane Mayi Yesu Khristu Wake, kuti alankhule ndi kumuuza kuti, “Inu ndinu AMENE ine ndinasankha. Inu ndinu AMENE ine ndimakukondani.Inu ndinu namwali Mkwatibwi Wanga wa mawu angwiro ,Ife Ndife M’MODZI.”
Kungomva chabe mawu amenewo, mitima yathu imadumphadumpha ndi chisangalalo. Kuganiza, padziko lonse lapansi, ndi ma mamiliyoni ndi mamiliyoni a anthu ake ambirimbiri, pali Mayi Yesu Khristu MMODZI yekha, ndipo INUYO ndinu Iye, amene Iye akubwelera.
Atate ali ndi malo amodzi osankhidwa opembedzera, Ambuye Yesu Khristu; Iye ndiye Mawu. Lero, pali malo amodzi okha omwe imfa ya uzimu siyingakanthe: Mawu. Imfa siyingakanthe Mawu, chifukwa Ndi Mawu Amoyo a Mulungu.
Vumbulutso lonse lathunthu la Mawu Amoyo lavumbulutsidwa kwa Mayi Yesu Khristu okha. Pali malo amodzi okha osankhidwa kumene Mayi Yesu Khristu angapiteko ndikumva Mawu ANGWIRO OLANKHULIDWA. Pali mneneri mmodzi yekha wosankhidwa kukhala Mawu a Mulungu. Pali malo amodzi okha omwe Mayi Yesu angapiteko ndikumva, PAKUTI ATERO AMBUYE: KUKANIKIZA KUSEWERA.
Kudzakhala kuli Kuwala cha mu nthawi ya madzulo, malo okha osankhidwa ndi Mulungu kuti uzipembedzapo. O, kodi Uthenga uwu wafika ku chiyani, kodi Iye achita chiyani? Ndipo mu tsiku lake kudzakhala kuli Kuwala pa nthawi ya madzulo, ndipo (chiyani?) kuti awalandire ana Ake akubwerera kwawo ku Dziko loona lolonjezedwa, ndi chizindikiro chomwe chija cha Lawi la Moto limene linawatsogolera ana a Israeli kudutsa mu chipululu.
Kodi ndimosamala motani momwe Mkwatibwi Wake ayenera kukhalira kuti atsatire ndikumva Liwu la Mwamuna Wake likulankhula naye. Pali malo AMODZI okha omwe ife tingapite ndikukhala otsimikiza handiredi peresenti. Pali Liwu limodzi lokha lomwe ife tayika komwe tikupita Kwamuyaya wathu.
Mayi Yesu Khristu amakhulupirira kuti Mawu omwe iye amamva pa matepi ndi Mawu a Mwamuna Wake.Iye Amakhulupirira kuti Mawu Ake safunikira kutanthauzira. Chifukwa chake, iye amakhulupirira kuti pali malo AMODZI okha operekedwa omwe iye angapite ndi kunena AMENI ku mawu aliwonse.Liwu la Mwamuna Wake pa matepi.
Kamodzinso kena, Mayi Yesu Khristu, ochokera kuzungulira padziko lonse lapansi, akhozanso kunena kuti, “Lero, Mawu awa olankhulidwa, ali kukwaniritsidwa”.
Wokondedwa Mulungu, kutali komwe kuwoloka zipululu uko mu Tucson, kupita mpaka mu California, mpaka mu Nevada ndi Idaho, kupita mpaka cha Kummawa ndi kozungulira, kutsikira mu Texas; pamene kuitanira uku kuli kuperekedwa, anthu atakhala mkati—mu mipingo yaying’ono, malo omwetsera mafuta, mmakomo, akumvetseramo.
Inu muli kuitanidwa kuti mudzamvetsere ndi Branham Tabernacle nthawi ya 12:00 PM, nthawi ya ku Jeffersonville, pamene tikumva Mulungu akulankhula ndi Mkwatibwi Wake wosankhidwa, Uthenga: “Malo Osankhidwa Ndi Mulungu Opembedzera” 65-0220.
Nthawi yomwe ife takhala tikuyiyembekezera mwachidwi komanso mofunitsitsa ndi ino. Ife tafika.Ife tikuwona iyo ikutambasulidwa pamaso pathu. Tsiku lililonse ulosi ukukwaniritsidwa, ndipo ife tinganene kuti: LERO LEMBA ILI LAKWANIRITSIDWA PA MASO PATHU.
Ndi kukondoweza Kwa Vumbulutso lotani likuchitika ndi mkwatibwi. Ndi Uthenga uliwonse womwe ife timamva, ife timamvelera mkatikati mwa mitima ndi miyoyo yathu, “Kodi izo zingatheke bwanji kukhala zazikulu mulimosemo komanso zabwino kwambiri, Ambuye?” Kenako Iye amabwera pakati pathu kachiwiri ndikutidzoza ife pamene ife tikumva Mawu Ake akutiitana ife nati, “Inu ndinu Wokondedwa wanga. Ine ndinakusankhani inu kuti mukhale Mkwatibwi Wanga. Monga Ine ndinakulonjezani inu, Ine ndikubwera chifukwa cha Inu. Ine Ndili pa njira yanga. Posachedwapa Ife tidzakhala limodzi ku muyaya.”
Ife tikufuula kuchokera kuzungulira padziko lonse lapansi, tikukwera Kumwamba ndi ma haleluya athu, ma ulemerero, matamando, ndi kulambira kwa Iye. Satana wagonjetsedwa. Atate wachotsa kukayikira kwathu konse, kusatsimikizika kwathu konse, zonse zoganizira. Ife tikhoza kulengeza ndi mtima wathu wonse ndi moyo wathu wonse, Ife NDIFE Mbewu Yachifumu Yapamwamba ya Abrahamu. Mkwatibwi Wachifumu kwa Mwana wa mwamuna Wachifumu wolonjezedwa.
Kukhalapo kwa Ambuye kwakhala kodabwitsa kwambiri pamene Iye akutivumbulutsira Mawu Ake kuposa kale lonse. Iye wagwirizanitsa Mkwatibwi Wake ndi Mawu Ake, natiyika ife mu Maganizo amodzi ndi mgwirizano umodzi ngati gulu limodzi, kumvetsera Liwu La Mulungu likulankhula ndi kutipanga ife kukhala angwiro ndi Mawu Ake.
Uthenga uliwonse umene ife timava uli ngati chitsime cha kasupe chomwe chikuphulika mkati mwa miyoyo yathu; chikutuluka, chikukankhira, ndi kutumphukira kuchokera ku Mpando wa Chifumu wa Mulungu.Ife Tikumwa ndi kumwa ndi kumwa, kuyipangitsanso miyoyo yathu kukhala yatsopano.
Abale ndi Alongo Anga, Ife ndife kukwaniritsidwa kwa Malemba omwe amati Iye adzakhala ndi namwali Mkwatibwi wa Mawu. Ife ndife: Lero Lemba ili lakwaniritsidwa.
Mulungu Mwiniwake analankhula kuchokera Kumwamba kwa mngelo Wake wachisanu ndi chiwiri nati, “Monga Yohane Mbatizi anatumizidwa kuti atsogolere Kubwera koyamba kwa Khristu, Uthenga wako udzatsogolera Kubwera kwa Iye kachiwiri, kudziko lonse lapansi.” Mkwatibwi anganene kuti: Lero Lemba ili lakwaniritsidwa.
Kodi ife tingamvetse kuti Liwu lomwelo la Mulungu lankhulidwa m’masiku athu ano kudzera m’milomo ya munthu, kujambulidwa, kusungidwa, ndi kusungidwira kuti iye athe kulankhula ndi aliyense wa ife, Pakuti Atero Ambuye? Iye wazipanga izo kukhala zotheka kuti ife sitimafunikila kuti tisatenge mawu a wina aliyense, osati malingaliro a wina, osati maganizo a wina, basi kungokhala pansi ndikumamvetsera Liwu Lake likuyankhula mwachindunji kwa ife Mawu Ake Oyera.
KODI CHOMWE CHIKUCHITIKA NDI CHIYANI LERO?
Ndipo M-w-a-n-a wa Mulungu yemweyo amene anabwera kummawa ndi kudzadzitsimikizira Yekha ngati Mulungu wowonetseredwa mu thupi, ndi M-w-a-n-a wa Mulungu yemweyo kumadzulo kwa dziko lapansi kuno, amene akudzizindikiritsa Yekha pakati pa mpingo usikuuno, yemweyo dzulo, lero, ndi kwanthawizonse. Kuwala kwa kumadzulo kwa Mwana kwafika. Lero Lemba ili lakwaniritsidwa pamaso pathu.
KODI IFE TILI MU MCHIFUNIRO CHANGWIRO CHA MULUNGU PAKUNENA NDI KUKHULUPIRIRA: “KUSEWERA MATEPI NDI NJIRA YOPEREKEDWA NDI MULUNGU KWA MKWATIBWI WAKE”?
Ine ndakhala pano m’mawa uno ndikumva kudzoza kumeneko pamene ndikumvetsera, kuwerenga ndikuphunzira Uthenga uwu umene Mkwatibwi adzamva Lamlungu. Thupi langa lonse ladzozedwa. Mtima wanga ukudzaza ndi chisangalalo chotelocho podziwa kuti, IFE TONSE TIDZASONKHANA PAMODZI KUCHOKERA PA DZIKO LONSE NDI KUDZOZA KOFANANA KOMWEKU. Ife Tidzakondwera, kutamanda Ambuye, nthawi imodzi, pamene IYE akulankhula ndi aliyense wa ife ndikuulula Mawu Ake.
Kudzoza kudzakhala kwakukulu kwambiri kotero kuti padzakhala kufuula ndi kukuwilira, “aleluya, ameni, lilemekezeke Dzina la Ambuye” padziko lonse lapansi nthawi imodzi, pamene tikukwera Kumwamba ndi matamando ndi kupembedza kwathu.
Kodi chidzakhala chikuchitika ndi n’chiyani? Mulungu adzakhala akugwirizanitsa ndi kulankhula ndi Mkwatibwi Wake.Ife tidzakhala Gawo limodzi, mu lingaliro limodzi ndi mgwirizano umodzi pamene Iye akudziulula ndi kudziwonetsera Yekha kwa ife.
Palibe malo akuluakulu omwe inu mungapiteko, palibe Liwu lalikulu lomwe inu mungamve; palibe kudzoza kwakukulu kuposa Liwu la Mulungu likulankhula nanu mwachindunji pa matepi.
Mulungu wakhala akuyang’anira Mawu Ake kuyambira pachiyambi ndipo wapereka malo omwe ana Ake onse angapiteko ndikumva Iye akulankhula ndikutanthawuzira Mawu Ake omwe. Malo omwe palibe kupenekera, chiyembekezo, kapena kudabwa; Iwo ndi malo operekedwa ndi Mulungu kuti mumve PAKUTI ATERO AMBUYE.
Zikakhala kuti izo Zavumbulutsidwa kwa inu, zimakhala ngati kuwala kwakukulu komwe kwayatsidwa mumtima mwanu ndi moyo wanu … Inu mumafuula, “icho ndi ichi. Ine Ndili kuchiwoona icho. Ine ndili MMODZI NDI MAWU. INE NDINE MAWU. INE NDINE MKWATIBWI. INE NDAFIKA.”
Icho Chikuchitika ndipo iwo sakudziwa. Ndi choncho. Mukuona? Inde bwana! Pakuti kumene kwafa nyama ndi kumene mphungu zidzasonkhana…?…Ndi zimene linanena. Kodi nyama yakufa kumene ndi chiyani? Mawu. Iye ndi Mawu, nyama yakufa, Khristu, Khristu mwa inu, yemweyo dzulo, lero ndi nthawi zonse. Izo zili zolondola bwanji!
Pamene ife tisonkhana kuti timve Mawu, zosamalira zathu zonse, nkhawa zathu zonse, mavuto athu onse, zimangotha momphweka. Ife timakondwera pamene tikuzindikira kuti ife tilibe chodela nkhawa nacho; ife ndife Mkwatibwi Wake. Iye siali nafe kokha, KOMA ALI MWA IFE. NDIFE MKWATIBWI WA MBEWU YA MAWU. Chilichonse ndi changwiro. Nthawi yake ndi yangwiro. Ife ndife angwiro.
Ife tili okhutira kwambiri ndi oyamikira kwambiri kunena kuti ife ndife Mawu Ake obadwa kwa namwali opangidwa kuwonetseredwa; Yesu Khristu yemweyo dzulo, lero, ndi kwa nthawi zonse, wokhala ndi moyo ndi kupezeka mkati mwathu. Aleluya!
Ife sitingathe kunyengelera pa MAWU AMODZI. Ife tiyenera kumva Mawu a Mulungu pa matepi.
Kodi inu munamuona mphungu akuvomerezera zosayenera? Ayi, bwana! Palibe zonyengerera mwa iye. Ndi momwenso Mkhristu weni weni amachitira. Iye siwolobodoka ayi. Amasaka mpakana atachipeza. Ameni. Inde, bwana! Iye mpakana atapeza chakudya chake. Iye amafuna manna atsopano. Adzafika pamenepo nakumba mpaka atachipeza Amauluka chokwera m’mwamba. Ngati sichiri m’chigwa chino, iye amakweranso m’mwamba pang’ono. Ukapita m’mwamba kwambiri, umaonanso kwambiri. Kotero ndi nthawi ya mphungu za tsiku lino kuti ziyambe kuuluka m’mwamba zedi, kukumba mu malonjezo a Mulungu, osati kumakhala moyo ndi chakudya cha akhwangwala chimene chinaphedwa zaka zapitazo. Tulukanimo m’menemo.
Khala okonzeka Mkwatibwi, ife tidzakhala tikudya Manna watsopano aja, titakhala pansi pa kudzoza kwakukulu komwe kulipo, Lamlungu lino nthawi ya 12:00 P.M, nthawi ya ku Jeffersonville, pamene tikumva: 65-0218 Mbewu Si ili Yolandira Cholowa Pamodzi Ndi Makoko.
Ife tikuitana Mkwatibwi kuchokera kuzungulira padziko lonse lapansi kuti adzalumikizane nafe kudya pa Njira Yangwiro Yoperekedwa ndi Mulungu ya lero. Malo okhawo kumene MKWATIBWI anganene kuti ameni ku Mawu aliwonse. Kumene kudzoza kwakukulu kwa Mzimu Woyera kumalankhula ndi kupangitsa Mkwatibwi Wake kukhala wangwiro mwa Kukanikiza Kusewera ndi kumva ndi kulandira Mawu Ake.
Ndi ulemu waukulu komanso mwayi waukulu wotani kunena kuti, “Ndife ana a nkhosa a Mulungu, amene Iye anawatumizira mthenga wake wachisanu ndi chiwiri kuti adzaitane ndikudyetsa Manna Ake osungidwa ndi obisika.”
Ife tikukhutitsidwa ndipo tikukhulupirira kuti Uthenga uwu ndi Liwu la Mulungu lomwe latumizidwa kuti lifikilitse ku ungwiro Mkwatibwi Wake. Ife tikukhulupirira kuti mankhusu akuchoka ku tirigu, ndipo tsopano Mkwatibwi Wake akukhala munkupezeka kwa Mwana, KUKANIKIZA KUSEWERA kuti ache.
Ndipo ndi chimene ife tadzera pano, mzanga, kudzakhala Pamaso pa Mwana kufikira gulu lathu lapang’ono la anthu pano, kufikira litachera kwa Khristu, ilo nkusandulika mkate pa gome Lake. Ndi chimene ine ndikufuna kuti iwo achite.
Aliyense amene sakhulupirira kuti KUKANIKIZA KUSEWERA ndi kumva Liwu la Mulungu lotsimikiziridwa likulankhula kuti ndiye Mawu ofunikira kwambiri omwe muyenera kumva, ndi munthu amene akuthawa pamaso pa Ambuye.
Iwe uyenera kuti ukomane nacho icho, kapena kuchitapo chinachake cha izo. Inu muli nawo udindo, wina aliyense ali nawo, ndipo inu muyenera kukomanizana nazo zinthu izi.
Kodi chobwereza ichi ndi chowona komanso chofunikira bwanji masiku ano. Pali magawano ochuluka pakati pa oitanidwa ake a Mulungu. Kodi ndikofunikira kwambiri kusewera matepi mu tchalitchi kuti mumve Liwu la Mulungu, kapena kodi tsopano ndikofunikira kwambiri kuti utumiki ulalikire Mawu?
Mulungu waitana ndi kuyika utumiki pano kuti usunge Mawu pamaso pa anthu. Iwo ndi Abusa. Mawu amaphunzitsa izi. Iwo ayenera kulemekezedwa ndi kupatsidwa ulemu monga anthu omwe Mulungu wawaitana ndi kuwaika. Ife Sitingathe, ndipo sitiyenera, kunena kuti Iwo si Mkwatibwi. Zimenezo ndi ZOLAKWIKA ndipo sizikugwirizana ndi zomwe mneneri anatiphunzitsa ife. Ine Ndamvapo anthu akunena kuti: “Ngati iwo sakusewera matepi m’matchalitchi awo, iwo ndi otsutsa Mawu.” Inu simukuyenera kunena chinthu monga chimenecho. Zimenezo zikundiwonetsa ine kuti inu muli ndi mzimu wolakwika.
Ndamva ena akunena kuti, “Onse ayenera kumalumikizidwa ndi BT kapena Iwo sali mu chifuniro cha Mulungu”. Inu simukuyenera kunena chinthu monga chimenecho. Mulungu yekha ndiye amadziwa amene ali ndi amene siali Mkwatibwi. Umenewo si mzimu wa Mkwatibwi kunena zinthu monga zimenezo.
Ngakhale ena mwa anthu omwe akulumikizidwa ndi ku BT akunena kuti, “ngati inu mupita kutchalitchi kukamvera matepi ndi kusamavera mu m’nyumba mwanu inu mukulakwitsa!” Zimenezo si zoona abale ndi alongo. Ngati inu mukunena zimenezo, SIYANI, mukulakwitsa. Aliyense ayenera kuchita monga momwe IYE AKUMVELELA KUTSOGOZEDWA NDI AMBUYE MOMWE ACHITIRE.
Atumiki ambiri amaona kuti kulalikira ndiyo njira yoperekedwa ndi Mulungu lero. Ife timangowona zinthu mosiyana, ndiko kulondola. Kodi M’bale Branham ndimochuluka motani anapanga kufanizila uku pa zimenezi? Tamumva pa mafunso ndi mayankho, pamene anthu ankalankhula za M’bale Jackson kuti akulakwitsa, anawadzudzula ponena chilichonse chotsutsana naye ndi mpingo wake.
Ine ndikungolalikira mwa njira ya kalata iyi zomwe ine ndimakhulupirira kuti ndi njira yoperekedwa ndi Mulungu ya Branham Tabernacle. Iwo ndi abale ndi alongo athu. Iwo amakonda Ambuye ndi Uthenga uwu. Umu ndi momwe amamvera kuti Ambuye akuwatsogolera. Ambuye alemekezeke.
Iwo amaziona izo mwanjira ina ndipo ife timazionaso mwa ina, Izo zilibwino. Ine sindingathe kuziona mwanjira yawo ndipo iwo sangaone yanga. Kwa ine, pali njira zambiri zomwe Mulungu wapereka, koma pali NJIRA IMODZI YANGWIRO, NDIPO KWA INE, NDIYO KUMAKANIKIZA KUSEWERA.
Ine ndikupemphera kuti musandive molakwika apa. Kusanjika manja ndi kupempherera anthu ndi zolondola ma peresenti handiredi molingana ndi Mawu. Kudzoza ndi mafuta ndi kupempherera odwala ndi Mawu a Mulungu molingana ndi Malemba. M’bale Branham analalikira ndi kutiphunzitsa ife tonse kukhala Mawu. Koma ine ndikufuna NJIRA YANGWIRO YA MULUNGU YOMWE IYE ANAYIPERELA …. INGOKHULUPIRIRANI CHIFUKWA MULUNGU ANANENA CHONCHO. Ndicho chimene ine ndikuyesetsa kuchita.
Koma tsopano pa machiritso, ndi chifundo cha Mulungu kuti IYE, “Ndi mikwingwirima Yake munachiritsidwa.” Tsopano, choyamba Mawu amanena choncho, zimenezo ziyenera kukhala zokwanira, koma ngati simukukhulupirira mu Mawu, ndiye kuti pali mphatso mu Mpingo, monga amuna omwe ali wodzonzedwa kudziwa momwe angaphunzitsire zimenezo, zomwe zidzapangitsa kuti zikhale zomveka kwa inu, ndiko kuti, ndi chikhulupiriro kukhulupirira.
Ine ndimakhulupirira mu utumiki wofutukuka pasanu. Ndimakhulupirira Mulungu anaitana anthu kuti azilalikira ndi kuphunzitsa Mawu. Koma, ine ndimakhulupirira kuti kumva Liwu la Mulungu pa matepi ndi NJIRA YANGWIRO KWA INE.
Pakumva matepi, ine sindiyenera kumvetsetsa, KUNGOKHULUPIRIRA MAWU ONSE AMENE INE NDIMAMVA. Palibe munthu, palibe mtumiki, palibe malo ena omwe ine ndingapiteko komwe ine ndimakhulupirira MAWU ONSE ndikuyika komwe ndikupita Kwamuyaya, koma matepi.
Kuyambira pachiyambi cha nthawi Mulungu sanapatse anthu ake mwayi ndi luso lodzimvera okha Mawu ake akulankhula milomo ndi khutu. Chinsinsi chilichonse chimawululidwa m’matepi. Funso lililonse limayankhidwa pa matepi. Chilichonse chomwe Mkwatibwi amafunika kuti akhale wangwiro chili pa matepi.
Mawu aliwonse olankhulidwa pa matepi ndi Mawu a Mulungu. Ine sindingamvetse kapena kufotokoza chilichonse, koma ine sindiyenera kutero. Amangofuna kuti ine ndinene AMEN KU MAWU ONSE, ndipo MATEPI ndi malo okhawo omwe ine ndingachite zimenezo.
Koma pamene—pamene iwe uyenera kuchita chinachake chosiyana, pamene iwe uyenera kuti uyime mmene iwe ukumverera kwa chimene iwe ukudziwa kuti ndicho Choonadi, apo ndi pamene pali gawo lovuta, apo ndi pamene kukhula kumabwera, pomwe apo.
Ine ndikukhulupirira kuti ndi zonse zomwe zili mwa ine, tili mu Chifuniro changwiro cha Mulungu ndipo ife tili m’chombo chopita ku Nineve. Ine ndikufuna kuti dziko lapansi libwere kudzayenda nafe pa chombo chathu ndi ife Lamlungu lino nthawi ya 12:00 PM, nthawi ya ku Jeffersonville, pamene ife tikumva Mulungu akulankhula ndi Ana a nkhosa ake.
M’bale Joseph Branham
Uthenga: 65-0217 “Munthu Kuthawa Pamaso Pa Ambuye”
Pali malo amodzi okha otsimikiziridwa komwe inu mungapite kukamva Ambuye akulankhula kudzera mwa mngelo Wake ndikukuuzani inu kuti, “Nthawi zonse kumbukirani, inu ndinu ana a Mulungu, Banja Lachifumu lokhala ndi Magazi Achifumu. Palibe Magazi abwino kuposa anu padziko lapansi. Inu ndinu ana anga, omwazikana padziko lonse lapansi, omwe ndawabalira kwa Khristu.”
Ife ndife Banja Lachifumu la Mulungu lokhala ndi Magazi Achifumu omwe akuyenda m’mitsempha yathu. Ana omwe abadwa kwa Khristu ndi Liwu la Mulungu likuyankhula kudzera mwa mneneri wake wamphamvu. Izo Sizingakhale bwino kuposa zimenezo abwenzi anga.
M’bale Branham, kodi Mkwatibwi adzafunika kusamukira ku Jeffersonville kapena ku Arizona kuti adzapite mu Mkwatulo?
Ndipo izo ndi zokayikitsa kwambiri ngati ziti zidzakhale mwanjira imeneyo, chifukwa Baibulo linati, “Adzakhala ali awiri mu kama; Ine ndidzatenga mmodzi ndi kumusiya mmodzi; ndi awiri ku munda, ndipo ine ndidzatenga mmodzi ndi kusiya mmodzi.” Mukuona? Kotero iwo mwinamwake…Kudutsa mdziko, iwo sadzakhala atasonkhana mu malo amodzi kuti akhale ochita zinthu mofanana. Koma magulu aang’ono a iwo adzakhala atamwazikana konse konse padziko lapansi.
Kotero mwakuthupi, sitidzakhala pamalo amodzi nthawi imodzi. Koma ulemerero kwa Mulungu, Iye anali ndi dongosolo lalikulu kwambiri lobweretsa pamodzi Mkwatibwi Wake.
Ife tikupempherera mipingo yonse ndi magulu amene asonkhana pozungulira zo—zo—zoyankhulira zazing’ono kunja kudutsa, kuchokera ku fukoli, njira yonse mpaka ku Gombe la Kumadzulo, kukwera mpaka ku mapiri a Arizona, kutsika mpaka ku zigwa za Texas, njira yonse mpaka ku Gombe la Kummawa, monse kudutsa dziko, Ambuye, kumene iwo asonkhana. Maora ambiri motalikana, ife tiri mu nthawi, koma, Ambuye, ife tiri limodzi usikuuno ngati chimango chimodzi, okhulupirira, tikuyembekezera Kudza kwa Mesiya.
Lero, sikuti Iye akusonkhanitsa Mkwatibwi Wake kuchokera ku dziko lino lokha, komanso Iye akutisonkhanitsa ife kuchokera ku ma kontinenti asanu ndi awiri a dziko lapansi. Kuchokera ku Africa mpaka ku Antarctica. North America ndi South America, Asia, Australia ndi Europe. Akusonkhanitsa ndikugwirizanitsa Mkwatibwi Wake ngati MMODZI kuti timve Liwu la Mulungu.
Iye anatiuza ife kuti tipite ku tchalitchi; ngakhale kumene amaphunzitsa theka la Mawu, kufikira MPAKA titapeza tchalitchi komwe amaphunzitsa MAWU ONSE. Mulungu alemekezeke Mkwatibwi tsopano wapeza malo amenewo, Mawu a Mulungu pa Tepi ndi MAWU ONSE.
Kaya inu muli ku tchalitchi chanu cha pa Nyumba cha Tape, tchalitchi chanu komwe mabanja ambiri amasonkhana, kapena m’nyumba m’nkhalango za Amazoni kapena Africa, kulikonse komwe mungathe Kukanikiza Kusewera kuti mumve Liwu la Mulungu likuyankhula nanu kuchokera ku kakamwa Kupita ku khutu, inu mudzakhala mu Tchalitchi cha MAWU ONSE.
Ife tapeza tchalitchi cha Mawu Onse ndipo ife tikukuyitanani inu kuti mudzalumikizane nafe Lamlungu lino nthawi ya 12:00 P.M., nthawi yaku Jeffersonville, pomwe tidzakhala tikumva: Mafunso ndi Mayankho #4 64-0830E.
Kodi wina angayike bwanji mkati mawu a chabe aumunthu chikondi ndi chisangalalo chomwe chili m’mitima mwathu kuti tidziwe Vumbulutso lenileni la Mawu Ake a tsiku lathu? Kuganiza, ife sitinali ndi chochita ndi icho, koma IYE, WAMKULU INE NDILI, mwa kusankha kwa IYE mwini, anatikonzeratu IFE kuti tikhale ndi chinthu chachikulu kwambiri chomwe Iye angatipatse, VUMBULUTSO LA MAWU AKE A TSIKU LATHU.
Iye anadikira, mpaka nthawi yonse itakwana, kuti apume mpweya wa moyo mwa ife, kotero kuti ife timumve Iye akulankhula nafe ndi kunena kuti:
Tsopano, ine ndayesa mwa kupambana kwanga k—k—kuti ndikuuzeni anthu inu ndi kukutsogolerani inu monga bambo angawatsogolere ana ake. Inu ndinu ana anga; ine ndakubalirani inu kwa Khristu kudzera mu Uthenga uwu umene ine ndikuulalikira. Mukuona? Ndipo i—i—ine ndikufuna inu kuti mukule kwathunthu kukhala ana okhwima, k—kapena ana. Ndipo ine ndikufuna kuti ndidzakuperekeni inu kwa Khristu tsiku limenelo, monga Paulo anati, “Namwali wangwiro.” Mulibe chinthu china mu Mawu amenewo koma chimene mtima wanu ungavomereze kuti “ameni” kwa icho.
Mulungu, polankhula kudzera mwa mngelo wake wamphamvu, akutilunjikitsa ndi kutitsogolera ife, Mkwatibwi wa Yesu Khristu. Ife ndife ana ake akucha mokwanira, namwali woyera mtima. Ndipo mwa chisomo Chake chodabwitsa, ife timavomereza Mawu aliwonse omwe ife timamva ndi AMEN! Ndi kutanthauzira kwangwiro kwa Mawu ndi chitsimikizo Chaumulungu!
Ngati Mawu omwe ife tikumva pa matepi ndi: kutanthauzira kwangwiro kwa Mawu, kodi Mkwatibwi wa Yesu Khristu akusowa chiyani china?…PALIBE!
Iye watisankha IFE, gulu lake laling’ono losankhidwa ndi dzanja, kuti tikhale ndi Vumbulutso lenileni la Mawu Ake la tsiku lathu lino. Ife ndi amene omwe Iye adasankha kukhala padziko lapansi, m’matupi a aumunthu, panthawi ya ulamuliro wa zana chikwi a mileniyamu.
Abwezi, tiyeni tikhazikike pa pamenepo mwa kamphindi.
Ife tidzakhala ndi thupi laulemerero padziko lapansi pomwe pano. Ife tidzakhala tikudya, kumwa, kumanga nyumba, kukhala monga momwe tikuchitira tsopano kwa zaka chikwi. Kudzakhala mbindikiro wa ukwati wathu komwe Mkwatibwi (IFE) ndi Mkwati (Ambuye Yesu Khristu) adzakhala MMODZI.
Ife tikuyang’anira ndi kuyembekezera nthawi yaulemerero iyi mphindi iliyonse ya tsiku lililonse. Ili pafupi kwambiri moti zikuoneka kuti tingathe kuikhudza. Ine ndikukhulupirira, ndi mtima wanga wonse, izi ndi zomwe zikuchitika kwa ife lero:
O, chilumikizano chauzimu chija cha Khristu ndi Mpingo Wake tsopano, pamene mnofu ukusandulika Mawu, ndipo Mawu akusandulika mnofu, kuwonetseredwa, kutsimikiziridwa. Basi zomwe Baibulo linati zikanadzachitika mu tsiku lino, izo zikuchitika, tsiku ndi tsiku. Bwanji, izo zikuwunjikana mofulumira kwambiri kunja uko, mu zipululu izo, ndi zinthu zomwe zikuchitika, mokuti ine sindingakhoze ngakhale kuyendera limodzi nazo izo. Ife tayandikira Kudza kwa Yesu, kuti alumikizane ndi Mpingo Wake, komwe Mawu akusandulika Mawu.
Iye akulumikiza Mkwatibwi Wake monga momwe Iye ananenera kuti adzachitira, ndipo ife ndi gawo la Icho. Ife tikuchiona icho Chikuchitika ndi maso athu. Ena sangachione kapena kuchimvetsa. Si cha iwo , ICHO NDI CHA IFE, ANA AKE OBADWA.
Mkwatibwi adali ndi mafunso oti afunse mneneri.
Kodi izo ndizokwanira kungomvera Liwu la Mulungu pa matepi okha? Mulungu adayankha ndipo adati: INDE!!
Kodi ana athu angapezenso zonse zomwe iwo akufuna kuti akhale Mkwatibwi wa Khristu pongomvera matepi: INDE!!
Kotero, Zonse zomwe Mkwatibwi amafuna zili PA MATEPI.
Ife tikudziwanso kuti Mulungu wapereka njira zina zambiri kwa ana Ake.
“Ndi mikwingwirima Yake inu munachiritsidwa.” Tsopano, choyamba Mawu amanena choncho, zimenezo ziyenera kukhala zokwanira, koma ngati simukukhulupirira mu Mawu, ndiye kuti pali mphatso mu Mpingo, monga amuna omwe ali ndi mzimu wodziwa momwe angaphunzitsire zimenezo, zomwe zidzapangitsa kuti izo zikhale zomveka kwa inu, ndiko kuti, ndi chikhulupiriro kukhulupirira.
Ife tikuthokoza kwambiri Mulungu wapereka amuna omwe ali odzonzedwa wodziwa momwe angaphunzitsire machiritso ndi Mawu Ake kuti awamveketse bwino kwa ena, koma Mkwatibwi Wake akufuna NJIRA YAKE YANGWIRO YOPEREKEDWA. Ndicho chokhacho chomwe IFE TIKUFUNA.
Ndikufuna kukuitanani kuti mubwere kulumikizana ndi Branham Tabernacle Lamlungu lino nthawi ya 12:00 PM, nthawi ya ku Jeffersonville, pamene tikumva: Mafunso ndi Mayankho #3 64-0830M.
Ndizosangalatsa bwanji kukhala ndi Vumbulutso la Mawu Ake ndikudziwa kuti ndife Mawu opangidwa thupi.
Kumene kuli nyama, ndi komwe Mkwatibwi adzasonkhana pamodzi. Ndipo kwa ife, pali malo amodzi okha angwiro omwe ife tingapezeko Manna ya tsopano amenewo: mwa kukanikiza kusewera ndikumva Liwu la Mulungu pa matepi.
Kakamba za Manna YATSOPANO, kodi tingayambe kuganiza zomwe tili nazo ku songa ya Chala chathu? Liwu lenieni la Mulungu likulankhula ndi Mkwatibwi Wake wokondedwa pa tepi, komwe kulibe kuganiza, kulibe kudabwa, kulibe kufunsa kapena kukayikira kuti yemwe tikumva ndi Mulungu, pogwiritsa ntchito liwu la munthu, kulankhula Pakuti Atero Ambuye kwa Mkwatibwi Wake.
Mwa vumbulutso, ife timakhulupirira kuti Ndi malo OKHAWO omwe ife tingapiteko ndi kupumulitsa miyoyo yathu kuti Mawu omwe tikumva si mawu a munthu, komanso sikutanthauzira kwake kapena lingaliro lake kapena wonjezeredwa kwa Iwo, koma iwo Ndi Mawu oyera a Mulungu akulankhula kwa ife ana a Mphungu, akuwulula Mawu Ake.
Ife timasonkhana mozungulira Mawu. Timawerenga Mawu Ake m’Mabaibulo athu. Ife iimamvanso anthu odzonzedwa ndi Mulungu ndinso amuna oyitanidwa odzazidwa ndi Mzimu Wake Woyera, akubwereza ndi kulalikira Mawu a Mulungu, koma mutsiku lathu , Mulungu wapereka malo momwe ife tingamve MAWU Ake ANGWIRO AKULANKHULIDWA, mwa kukanikiza kusewera.
Atate Koteronso amapatsanso Mkwatibwi Wake mwayi wofunsa mafunso omwe anali pamtima pathu kuti tikhale ndi yankho langwiro:
Kodi Satana angagwiritse ntchito mphatso ya malilime kapena ulosi mwa munthu amene ali ndi Mzimu Woyera?
Kodi Yesu ankatanthauza chiyani mu Mateyu 12, vesi 32?
Chonde fotokozani 1 Akorinto 13:8-12.
Kodi akazi ndiwololedwa kugwira ntchito mmabwalo awunyinji wa anthu pomwe iwo alinaye mwamuna ndi ana athanzi labwinobwino?
Kodi n’kulakwa kuti mkazi azimanga tsitsi lake?
Mulungu wapereka njira zambiri zodalitsira ndi kulimbikitsira Mkwatibwi Wake, koma pali malo amodzi okhawo omwe wapereka komwe Mkwatibwi Wake angakhale ndi chidaliro chama peresenti 100 kuti chomwe iwo akumva ndi MAWU AKE ANGWIRO. Kasupe Mmodzi wa Madzi Amoyo komwe Ana Amphungu amatha kumwa kuchokera ku iye komwe kulibe kuthekera kwa kuipitsidwa kulikonse. KUKANIKIZA KUSEWERA.
Ine ndikukuitanani inu kuti mudzamwe kuchokera ku Kasupe ameneyo Lamlungu lino nthawi ya 12:00 PM, nthawi ya ku Jeffersonville, komwe ife tidzava 64-0823E “Mafunso ndi Mayankho #2.”
Moni kwa Mkwatibwi wa Yesu Khristu kuchokera kuzungulira padziko lonse lapansi, omwe amakhulupirira kuti Branham Tabernacle, Liwu la Mulungu, ndi tchalitchi chawo cha kwawo komwe iwo akudyetsedwa mwauzimu ndi Mana obisika omwe asungidwa ndi kusungidwira Mkwatibwi wa Khristu.
Kuno ndi kwathu kokhazikika; kuno ndi likulu langa; kuno ndi kumene ife tinakhazikikako. Tsopano, sungani zimenezo mmalingaliro ziribe kanthu chomwe chingachitike. Tsopano, ngati ndinu anzeru, mugwira chinachake. Ziribe kanthu chomwe chingachitike, lino ndi likulu lathu, pomwe pano!
Okhulupirira ambiri nthawi zonse akhala osamvetsetsa kapena kuyika lingaliro lawo kapena kutanthauzira kwawo ku zomwe mneneri ananena apa, koma akuuza Mkwatibwi molunjika, “ngati Inu muli anzeru, mugwira china chake, ili ndiye likulu lathu, komwe kuno!”
Kodi Iye ankatanthauza chiyani pa zimenezo?
pomwe m’bale Branham anali pano, ambiri sanamumvetse bwino Iye ndipo ankaganiza kuti Mkwatibwi ayenera kupita ku Arizona ndi kumutsatira iye kumeneko, kuti adzapite mu Mkwatulo. M’bale Branham anawayankha momveka bwino kuti: KHALANI PANO, AWA NDIWO MALO.
Anthu ananyamuka kuchokera kulikonse mu United States kupita ku Arizona, koma iye anawauza momveka bwino kuti: Khalani pomwe pano, awa ndiwo malowo!
Khalani ku Jeffersonville? Ndicho chimene ananena!
Vumbulutso langa ndi lakuti, anali Mulungu, akulankhula kudzera mwa mneneri wake ndikuuza anthu kuti, “KHALANI NDI MATEPI.” Awo NDIWO MALOWO!
Iye kotero anakwiya ndipo iye anati ankayenera kuchitapo chinachake ndi anthu onsewo.Kodi iye ayenera kuti anachita chiyani? Kodi ndi ku tchalitchi chiti komwe Iye akanawatumizako iwo? Kodi iwo ankayenera kupita kuti? Kodi M’bale Branham anati iye ayenera kuti anachita chiyani?
Kotero tsopano, ine ndikuyenera ndiwabweretse ana amenewo kuno kuti adzapeze chinachake choti adzadye. Iwo ali kumusi uko mchipululu akuvutika ndi njala.
Iye sananene kuti iwo ankafunikira kupita kutchalitchi chapafupi ndikukatengako tizidutswa tating’onoting’ono tomwe iwo angadye. Iye anati ankayenera KUWABWERETSELANSO KUNO chinachake choti adzadye, apo kupanda kutero AKANAFA NDI NJALA.
VUMBULUTSO LANGA, ABWENZI.
Tsopano, musatinso kachiwiri musamuvetsenso molakwika, kapena kunena zomwe iye sananene, ponena kuti, “M’bale Branham amafuna kuti wokhulupirira aliyense apite kukakhala ku Jeffersonville kuti akhale Mkwatibwi.” M’bale Branham ankadziwa anthu onsewo, ndipo wokhulupirira ALIYENSE wochokera padziko lonse lapansi, sakanatha kuchoka ndikukhala ku Jeffersonville. Zimenezo sizikanatheka. Ndiye iye ankatanthauza chiyani? Iye Anali KUGWIRIZANITSA Mkwatibwi wa Khristu mozungulira matepi omwe anajambulidwa ndi kusungidwa kuti Mkwatibwi adye.
Uthenga uwu, Liwu ili, ndi Mawu Olankhulidwa ndi Mulungu lero ndipo ilo lidzagwirizanitsa ndi kumupanga Mkwatibwi wa Yesu Khristu kukhala wangwiro.
Nyama ndi chimene mphungu zimadya. Tsopano, mphungu imafanizidwa mu Baibulo, ngati mneneri. Mneneri ndi mphungu. Mulungu—Mulungu amadzitcha Yekha mphungu, ndipo ndife “ana a mphungu” ndiye, o—okhulupirira. Inu mukuona? Ndipo nyama imene izo zimadya ndi chiyani? Ndi Mawu. Kulikonse kumene kuli Mawu, chikhalidwe chenicheni cha mbalame chidzadziwonetsera chokha.
Kodi Mawu a Ambuye oyera ali kuti , otsimikizilidwa, osakhala osamvetsetseka, Pakuti Atero Ambuye wa lero? Pali malo amodzi okha, Matepi.
Ndikhoza kupitiriza, ndi chobwereza pa pachobwereza, koma Uthenga uwu ndi zomwe M’bale Branham ananena zimatenga vumbulutso kuchokera kwa Mulungu. Tiyenera kuwerenga pakati pa mizere ndi vumbulutso, koma muzinena zomwe iye adanena. Pakuti Ndi Mawu OYERA.
Mafunso ndi Mayankho a lero ndi zomwe NDIMAKHULUPIRIRA.
Masiku ano, atumiki ambiri akuuza anthu kuti pokhala ndi Tchalitchi cha Mnyumba cha Tepi ife tasiya Mawu ndi zomwe M’bale Branham anati ife tichite. Amavelera kuti ife tiyenera kupita ku zomwe iwo amazitcha ndikuzitenga ngati tchalitchi.
“Tsopano, inu muzipita ku tchalitchi china chabwino cha Uthenga wonse ndipo mukazipezere tchalitchi cha kwanuko.”
Ndipo ine ndimakhulupirira zimenezo ndi mtima wanga wonse, chifukwa iye anatero. Koma ine ndikukhulupirira kuti ife tikuchita zimenezo mwa KUKHALA NDI TCHALITCHI CHA PA NYUMBA CHA TEPI. Malo athu si omwe ali ofunika kwa Ambuye. Imeneyo ndi nyumba chabe. Koma ntchito yathu kwa Ambuye ndikukhalabe ndi Mawu Ake, OSATI MALO KAPENA NYUMBA. Malowo sapulumutsa ndi kupangitsa Mkwatibwi kukhala wangwiro, MAWU AMACHITA.
Ngati ndipita ku nyumba ya tchalitchi, koma ayiwala CHINTHU CHACHIKULU: kumva Liwu la Mulungu mwa kukanikiza Kusewera, ndipo angolowetsapo m’malo mwake pongomva KOKHA atumiki akulalikira Uthenga, kodi zimenezo zidzakukhutiritsani kotheratu ndi kudyetsa moyo wanu wonse? Zingakhutiritse moyo wanu, m’bale wanga ndiso mlongo wanga, koma sizidzakhutiritsa Mkwatibwi.
Ndiloleni ine nditsindike apa ndikunena kuti pali anthu zikwizikwi omwe alibe nyumba ya tchalitchi yoti apiteko. Kodi iwo atayika? Ngati iwo alibe m’busa kapena tchalitchi, kodi zimenezo zikutanthauza kuti iwo sangakhale Mkwatibwi? Ngati inu mukukhala pamtunda wa makilomita 100 kuchokera ku nyumba ya tchalitchi, kodi inu mukuyenera kupita ku tchalitchi chimenecho? Koma ngati ine ndikukhala kutali, ine sindiyenera kutero? Ine Ndiyenera kulumikizidwa ku mlaliki, koma ine sindingathe kulumikizidwa ku matepi? Nyumba yowoneka ndi maso ndi imene mneneri akunena kuti ndi chinthu chofunika kwambiri chomwe ife tiyenera kupitako?
Kachiwirinso, Ine ndimakhulupirira kupita kutchalitchi. Pali matchalitchi ambiri kuzungulira padziko lonse lapansi omwe akuika matepi moyambilira pa maguwa awo, Ambuye atamandike. Kodi ine ndikukhulupirira kuti muyenera kukhala panyumba kapena inu simuli Mkwatibwi? AYI, AYI, AYI….ine sindinaganizepo chimenecho, ine sindinakhulupirirepo chimenecho. Ine Ndikungofuna kuti MUZIKANIKIZA KUSEWERA mosatengela kuti kaya inu muli kuti kapena ndi tchalitchi chiti chomwe inu mukupita.
Ngati inu mulibe vumbulutso la zomwe iye akunena, ndiye kuti inu munganene momveka bwino kuti, “Ine Sindiyenera kumvera M’bale Branham ngakhaleso kapena KUVOMEREZA zonse zomwe iye akunena. Ngakhaleso Iye Ananena choncho, pali amuna ena ambiri oitanidwa ndi Mulungu.”
Kazipitaniko. Ife tikuzindikira apa, akuti, “Kodi ife tizipita ku mpingo wina umene sugwirizana ndi inu?” Ndithudi, ine sindi…Ine si nsangalabwi yokhayo mmphepete mwa nyanja, inu mukudziwa. Alipo—alipo amuna ena a umulungu konsekonse; ndikukhulupirira kuti ndine mmodzi wa iwo.
Mawu a Mulungu pa matepi ndiyo SANGALABWI YANGA, THANTHWE LANGA. Ndi Liwu lomwe ndikufuna kumva komanso Liwu lomwe ndikufuna kuti Branham Tabernacle imve.
Ngati inu mukufuna kulumikizana nafe, Inu muli olandiridwa kwambiri, abale ndi alongo anga. Mudzalumikizane nafe Lamlungu nthawi ya 12:00 p.m., nthawi ya ku Jeffersonville, pamene tidzava Liwu la Mulungu likulankhula ndikuyankha mafunso ambiri omwe mungakhale nawo mumtima mwanu. Ndipo mverani nokha ngati zomwe ine ndanena m’kalata iyi sizikugwirizana ndi Mawu ndiso ngati ine sindinamvetse bwino zomwe Mulungu akunena kwa Mkwatibwi Wake.
Zimene iye akunena pa matepi ndi Pakuti Atero Ambuye. Osati zomwe ine ndikunena ndi zomwe iye akunena, kapena zomwe ine ndikukhulupirira kuti iye akunena, ndipo Mulungu YEKHA ndi amene angakupatseni inu Vumbulutso lolondola.