Category Archives: Uncategorized

23-0129 Mulungu Wa M’badwo Woipa Uno

Uthenga: 65-0801M Mulungu Wa M’badwo Woipa Uno

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Namwali wamung’ono wa Khristu, Mawu, Nkhosa,

Sitingakhale chinanso. Sitingamve china chilichonse. Sitikudziwa china chilichonse. Sitikufuna china chilichonse. Kumene kuli Nyama yatsopano, KUTYAKA KULIZA, amene ali Mawu a nyengo, kumeneko mphungu zidzasonkhana. Mawu obwera kumoyo mwa ife.

Sitili ndi wina aliyense! Inu ndinu anthu opatulidwa, oyera kwa Ambuye, odzipereka kwa Mawu ndi Mzimu wa Mulungu, kuti mubale chipatso cha lonjezo Lake la tsiku lino. Timakula nthawi zonse ndi kukhwima pomva Mau a Mulungu.

Mneneri anatiuza ife kuti tiloze mmbuyo ku matepi awa. Ngati muli ndi makina a tepi, sonkhanitsani gulu la anthu ndi kutyaka iyo, ndipo mvetserani mwatchifupi. Mvetserani ku Liwu Lake, zomwe Iye akutiuza ife. Mawu a Mulungu safuna kutanthauzira; Iye amachita kutanthauzira Kwake Kwake. “Ine ndine Liwu la Mulungu kwa inu.”

Ndipo ili ndi Ilo, Baibulo, palibe mawu amodzi oti awonjezedwe kwa Ilo kapena kuchotsedwa kwa Ilo. Ingokhalani kumene ndi Liwu limenelo. “Mlendo sangamutsatire,”

Kodi zingatheke bwanji kuti munthu asaone Njira yoperekedwa ndi Mulungu masiku ano? Koma ulemerero kwa Mulungu, ife tikhoza kuchiwona Icho, chifukwa ndife osankhidwa kuti tiziwone Izo. Ife sitinga, ndipo ife sitingakhoze kunyengedwa, chifukwa ife ndife Mawu Ake owonetseredwa.

Abale ndi alongo, lakani izi zilowetsedwa mphindi imodzi chabe, NDIFE MAWU AKUONETSEDWA!! Mulungu Mwiniwake, akuyankhula kupitira mu milomo ya munthu, akutiuza ife IFE NDIFE MAWU. Sitiyenera kuopa chilichonse. Zonse zomwe tikufuna ndi zathu.

Mlungu uliwonse timayembekezera kuti Yehova adzatichezera. Ife tiribe malo pano oti tikhazikike aliyense, ngakhalenso aliyense sangakhoze kubwera ku Jeffersonville, kodi ife timaba tumizira iwo Mawu kupitira mu njira ya intaneti.

Ife tiri mumanyumba zathu, mu mipingo yathu, m’magalimoto athu, tasonkhana mozungulira maikolofoni athu ku chokera dziko lonse, kuyembekezera Kubwela kwa Ambuye.

Iwo asonkhana pamodzi nafe ku Africa, kuyembekezera Kubwela kwa Ambuye. Iwo asonkhana pamodzi nafe ku Mexico, kuyembekezera Kubwela kwa Ambuye. Ku Ulaya, Scandinavia, Australia, Middle East, South America, kuchokera konse mu dziko lapansi, kuyembekezera Kubwela kwa Ambuye.

Ndipo ife tasonkhana kuno ku mpingo wakwathu, Kachisi, tikuyembekezera Kubwela kwa Ambuye. Ife tiri maningi ochuluka mu nthawi, koma ife tiri pamodzi monga chigawo chimodzi, okhulupirira, kumvetsera ku Liwu la Mulungu, kuyembekezera Kubwea kwa Mesiya.

Ndife anthu oyitanidwa ndi osankhidwa a Mulungu kuchokera mu m’badwo woyipa uno chifukwa cha Dzina Lake. Ife tikuyesedwa ndi kutsimikiziridwa kwa Satana kuti ndife Mawu. Ndife gawo la Mtengo wa Mkwati Wapachiyambi uwo. Ife tikuwona moyo wathu ukuwonetseredwa ndi Mawu amenewo.

Ndishosavuta kuti aliyense akhulupirire kuti Yesu anali yankho lachindunji ku ulosi uliwonse womwe uyenera kukwaniritsidwa mwa Iye, chifukwa akuyang’ana mmbuyo kuti awone zikuchitika. Koma mu m’badwo woipa wamakono uno, iwo akuchita chinthu chomwecho chimene iwo ankachichita apo, pochitanthauzira Icho mwanjira ina, ndipo awapangitsa anthu kupita mu zosokeretsa zamphamvu kuti akhulupirire bodza. Ngati iwo akanakhoza kokha kuzindikira Iwo ali Mawu omwewo a m’badwo uno akuwonetseredwa.

Pali chinthu chimodzi chokha chimene chingakhoze kubweretsa Mkwati pamodzi, Uthenga uwu. Pali chinthu chimodzi chokha chimene ife tonse tingagwirizane nacho, Uthenga uwu. Pali Liwu limodzi lokha limene latsimikiziridwa kuti liri KULANKULA AMBUYE, Liwu la Mulungu pa tepi.

Tsopano, mipingo yozizira basi, yofunda, yokhuthala, ndi zina zotero, za fioloje zopangidwa ndi anthu, zomwe sizikana; Osankhidwa sakanapereka tcheru kwa izo. Koma zili pamwamba apo pafupifupi ngati zenizeni. Kungosiya Mawu amodzi ndi zonse zomwe muyenera kuchita. Lonjezedwa za m’badwo; nthawi yabwino kwambiri! Akhristu, kulikonse, samalani ku nthawi limene tikukhalamo! Lembani pansi, ndi kuwerenga, ndi kumvetsera pafupi.

Mulungu wa m’badwo woipa uwu akuchita zonse zomwe angathe kuti anyenge anthu powasunga Mawu Ake otsimikiziridwa kwa iwo. Iye akuyesera kuti awapangitse iwo kusakhulupirira Mawu amodzi okha, monga iye anachitira kwa Eva pachiyambi.

Koma Mkwati wa Mawu wa Khristu akubwera ku Mutu. Timabwereranso kwa Mnzathu komwe tinayambira. Nthawi yotuluka yayandikira. Mulungu Abwela ku Mkwati Wake yemwe amakhala ndi Mawu Ake.

Mzimu Woyera uli pano ukuitana Mkwati wa Khristu. Iye akuchita izo mwa kutsimikizira Mawu Ake a lonjezo kwa Iye, a m’badwo uno, kusonyeza kuti Iwo ndi Khristu.

Palibe chachikulu kuchila kukhala olumikizana ndi Mkwati kuzungulira dziko, kumvetsera ku Liwu la Mulungu likuyankhula molunjika kwa inu. Palibe chifukwa choyembekezera, kudabwa kapena kupemphera zomwe mukumva ndi zoona. Pakuti Iwo ali OWLIKIRIKA YEKHA, KULANKULA MAWU YA AMBUYE.

Bwerani mudzatimvetsere:

Ndipo zitatha izi ndinaona mngelo wina akutsika Kumwamba, wakukhala nao mphamvu yaikuru; ndipo dziko lapansi linawalitsidwa ndi ulemerero wake.

Pa 12:00 P.M., nthawi ya Jeffersonville, monga ife tikumva: MULUNGU WANTHAWI YOIPA INO 65-0801M.

Bro. Joseph Branham

Malemba yo werenge pamene mukalibe kuvelera Uthenga:

Mateyu 24 mutu 27:15-23
Luka 17:30 St
Yohane 1:1/14:12
Machitidwe 10:47-48
1 Akorinto 4:1-5; chaputala 14
2 Akorinto 4:1-6
Agalatiya 1:1-4
Aefeso 2:1-2/4:30
2 Atesalonika 2:2-4 / 2:11
Ahebri mutu 7
1 Yohane chaputala 1 / 3:10 / 4:4-5
Chibvumbulutso 3:14/13:4/Mitu 6-8 ndi 11-12/18:1-5
Miyambo 3:5
Yesaya 14:12-14

23-0115 Iwo Odzozedwawo Pa Nthawi Yotsiriza

Uthenga: 65-0725M Iwo Odzozedwawo Pa Nthawi Yotsiriza

PDF

BranhamTabernacle.org

Okondedwa nkhosa Osonkhanina Mu khola,

Ndine wokhutitsidwa ndi woyamikira kwambiri kwa Ambuye kusonkhana ndi aliyense wa inu mu Khola la Nkhosa la Mulungu mlungu uliwonse, kumene timabisidwa mobisika, kudya ndi kukhala ndi Chakudya Chobisika chimenecho. Ndi Vumbulutso la Yesu Khristu, kudzitsimikizira ndi kudziulula Yekha kwa ife.

Iye wadzibisa Yekha kuti ena ayang’ana kumene pa Iwo ndipo sachiwona Iwo, koma kwa ife, Mkwati Wake wosankhidwa, ife tikuwona Iwo mwa mbalambanda ndi kukhulupirira Mawu aliwonse. Ife takhala ndi Mawu Ake ndi mneneri Wake monga iwo ali umodzi ndi umodzi.

Ndipo ngati inu muli mwana wa Mulungu, inu muzakhala ndi mneneri wa Baibulo ili. Ndi Mawu.

Aneneri ambiri odzozedwa masiku ano amati “Ndi Mzimu Woyera umene uyenera kukhala nawo, osati mneneri.” Monga aneneri akale, ngati ife tiri ndi funso, payenera kukhala yankho yamunshye. Ife tiyenera kuyenda KU MAWU kuti tikawone zomwe mneneri patsogolo pathu ananena.

Koma pali Mzimu wazohona wa Khristu, ndipo ndiwo Mawu osandulika thupi momwe analonjezera kuchita.

UMODZI weniweni wa Khristu Mzimu umene Iye analonjeza, Malaki 4, Luka 17, Mwana wa Munthu akudziulula Yekha mu thupi la munthu.

Inde, alipo amuna odzozedwa. Inde, ali nako kuitanidwa. Inde, iwo ali ndi Mzimu Woyera weniweni. Inde, ali ndi zolinga ndi zolinga zabwino.

Ndiye tingadziŵe bwanji chabwino ndi choipa?

Zindikirani, iwo akuwoneka chimodzimodzi. Iwo anadzozedwa chimodzimodzi. Koma zindikirani, “Ndi chipatso chawo…”

Ndimasonda kunena zinthu izi koma nthawi lachedwa ndipo nthawi ikuthawa. Izi ndi zimene zikunenedwa ndi kulalikidwa lero ndi mimbulu yolusa ija Paulo anachenjeza mpingo, ndi odzozedwa abodza M’bale Branham anati adzabwera. Iwo ali pano pakati pathu, monga ananenera.

Nayi gawo la kalata yolembedwa kuchokera kwa mtumiki. Chipatso chawo chikuyesa kukayikira mneneri wa Mulungu. Amachenjeza anthu awo kuti ife ndife opembedza potsatira Mneneri ndi Kutyanka Kuliza.

Mvetserani momwe izi ziliri zachinyengo.

Ndi makala wolakwilisidwa kuti chiwanda ichi chalowa muuthenga wathu kotero kuti tsopano timaitana afalitsa za maulaliki a William Branham kuti NDI MAWU A MULUNGU. William Branham sanali liwu lenileni la Mulungu, koma liwu la munthu amene Mulungu anamugwiritsa ntchito. Baibulo silimanena kuti iye anali liwu la Mulungu, koma Baibulo limamutchula iye monga liwu la mngelo wa 7. ( Chiv 3:14; 10:7 ).

Tiyeni tipite ku MAWU ndikulola mneneri wa Mulungu kuvumbulutsa chiphunzitso chonyenga ichi.

Ngati ndakulakwirani ndikunena zimenezo, ndikhululukireni, koma, ndinamva kuti mwina ndakhumudwa, koma, INE NDINE MAWU A MULUNGU KWA INU.

Tsopano kodi inu mukhulupirira ndani, mneneri wodzozedwa wabodza uyu, kapena MTUMIKI WA NGELO WACHISANU NDI CHIWIRI WA MULUNGU? Inu mungakhoze bwanji kukhala pansi pa mtumiki aliyense yemwe angakhulupirire kapena kukuphunzitsani inu zinthu izi? Inu chilibwino mulowe mu Mawu pamene nthawi ikaliko.

Kulakwitsa koyipa kwapangidwa ndi gulu la uthenga pomuyesa William Branham kukhala chishintilizo. William Branham sanali konse chishintilizo! Mawu a Mulungu ndiwo chishintilizo.

Amen, Mawu a Mulungu NDI chishintilizo chathu. Kodi Mawu anabwela kwa ndani, inu kapena IYE? Kodi wotanthauzira mwaumulungu wa MAWU A MULUNGU ndi ndani, inu kapena IYE? Ndi ndani yemwe Lawi la Moto linamutsimikizira kuti ali NDI MAWU AMBUYE, inu kapena IYE?

Chifukwa iwe umapeza amuna awiri, iwe uli nawo maganizo awiri.

Ife sitikufuna amuna awiri kapena maganizo awo, ife tifuna zomwe mneneri wa Mulungu ananena pa tepi.

Ndipo uyenera kufika ku chishintilizo chimodzi, ndipo chishintilizo changa ndi Mawu, Baibulo.

Ndi zimenezo, monga momwe munanenera, Baibulo ndi lake ndi chishintilizo lathu, koma kenako akuti:

Ndikudziwa kuti inu, abale athu, mumayang’ana kwa ine kuti ndine chishintilizo chanu.

Kotero yembekezani kamphindi, izo zikumveka zosiyana ndi zomwe MUNANENA. Iye anati ife timayang’ana kwa iye kukhala Chishintilizo chathu.

Molingana ngati ndimatsatira Mulungu, monga Paulo ananenera m’Malemba, “Inu munditsate ine, monga ine ndimatsatira Khristu.”

Kodi ameneyo si wodzozedwa? Kodi iye sankadziwa zimene ankanena?

Kodi mneneri wa Mulungu anatiuza chiyani sabata yatha?

Ife tikupeza kuti pamene munthu abwera, wotumizidwa kuchokera kwa Mulungu, wodzozedwa ndi Mulungu, ndi MAWU AMBUYE owona, uthenga ndi mthenga zimakhala mmodzi ndi mmodzi.

Anati simungawalekanitse, ali chinthu chimodzimodzi, koma inu mukuti tiyenera?

William Branham sali wosiyana ndi munthu aliyense wachivundi, pakuti iye anali munthu wa zikhumbo, monga analiri Eliya.

Ameni, iye anali munthu motsimikiza, koma iye anali MUNTHU amene Mulungu anamusankha kuti amuululireko Mawu Ake onse, ndi kutitsogolera ife ku Dziko Lolonjezedwa. Iye anali mmodzi yemwe Mulungu anati, apangitseni anthu kuti akukhulupirireni INU.

Chinthu chomwecho, odzozedwa, kulalikira Uthenga wa pentekoste, koma kukana lonjezo la tsiku-lino la Mawu kukhala likutsimikiziridwa, “Yesu Khristu yemweyo dzulo, lero, ndi nthawizonse.”

Kodi ife tingadziwe bwanji kusiyana kwake ngati iwo ali odzozedwa owona a Mzimu Woyera? Anatipatsa zitsanzo kuti tidziwe aneneri onyenga kuchokera kwa mneneri woona.

Balamu ndi Mose. Mikaya ndi Zedekiya. Yeremiya ndi
Hananiya. Muzochitika zonse onse awiri anali aneneri odzozedwa a Mulungu, koma kodi iye anatiuza kuti tichite chiyani, KHALANI NDI MNENERI WA MULUNGU WOYENZEKEZEKA. Imeneyi ndi njira YOKHALA yotsimikizira kuti mukutsatira Njira yoperekedwa ndi Mulungu, ndipo muli mu chifuniro Chake chanbwino.

Ine ndine mmodzi yekha amene ali pafupi pamene Iye azichita izo. Ine ndinali liwu lokha limene Iye ankagwiritsa ntchito, kuti azinene Izo. Sizinali zomwe ndimadziwa; ndi chimene ine ndinangodzipereka kwa icho ndekha, chimene Iye anachiyankhula nacho.

Ndizo zonse Mkwati akufuna ndi zosowa. Liwu Limodzi. Mneneri umodzi. Uthenga umodzi. Mtumiki umodzi.

O Atate, ndife othokoza bwanji chifukwa cha chisomo Chanu ndi chifundo kwa ife. Munatiuza kuti palibe chovuta ndi Inu. Palibe chovuta ndi ife. Pakuti zinthu zonse ndi zotheka kwa iwo amene akhulupirira, ndipo ife TIKHULUPIRIRA.

Bwerani mudzabwere nafe Lamlungu nthawi ya 12:00 P.M., nthawi ya Jeffersonville, pamene tili ndi Liwu losankhidwa ndi Mulungu limatiuza zonse za Odzozedwa Pa Nthawi Yotsiriza 65-0725M.

Bro. Joseph Branham

23-0108 Chakudya Chauzimu Mu Nyengo Yake

Uthenga: 65-0718E Chakudya Chauzimu Mu Nyengo Yake

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Wosakila

Pali chitsime cha Chivumbulutso chomwe chikutumphuka mkati mwathu kupambana kale lonse. Ife tamva Uthenga uwu moyo wathu wonse, ndipo nthawizonse takhala tikukhulupirira Mawu aliwonse, koma TSOPANO Iwo wakhala akuwonetseredwa mwa ife kupambana kale.

Tsopano ndi nthawi, tsopano ndi nyengo yomwe ife tikudyera pa zinthu zobisika za Mulungu zomwe zabisika kwa dziko. Chinthu chimene anthu amaseka ndi chinthu chimene timapempherera. Chinthu chimene anthu amaitana “kufunta,” timaitana “Chachikulu!” Mulungu watiululira kuti pali njira imodzi yokha yoperekedwa kunkala Mkwati Wake, KUTYANKA KULIZA.

Koma zikomo kwa Mulungu, tili ndi Chakudya chobisika, Chakudya chauzimu chomwe tikukhala pa ubwino ndi chifundo cha vumbulutso la Yesu Khristu m’masiku otsiriza ano, kudzitsimikizira ekha pakati pa anthu Ake.

Ndi Uthenga uliwonse umene Mkwati amamva, Amatsimikizira kwa ife kuti ndicho chifuniro Chake chabwino. Sizimene TIKUGANIZA kuti Iye akulankhula, komanso sizomwe TIKUGANIZA Izo zikutanthauza, NDI EXAKATILI zimene Iye Akunena ndipo ena sangathe kuziwona; iwo anavalika manso. Mulungu wazibisa Izo. Iwo amayang’ana kumene pa Iwo, koma samawawona Iwo. Kwa ife, NDI ZONSE TIZIONA.

Pamene tikusonkhana sabata iliyonse, sitingathe kunva zomwe Iye atiuze ndi kutiululira. Lamlungu lino, Iye satipatsa ife tinthu tating’ono tobisika, Atipatsa ife malo okhala ndi amayi ndi KULIBULA mobwerezabwereza kuti titsimikizire kuti tapeza.

Mneneri animals maningi mupulezensi ya Mulungu, aneneri a Chipangano Chakale, kapena nthawi iliyonse, pamene iwo amakhala mupulezensi ya Mulungu mpaka iwo akhala Mawu, Uthenga wawo ndi Mawu yameneo. Ndipo, kumbukirani, iye anati, “ KULANKULA KWA AMBUYE.”

Ife tikupeza kuti pamene munthu abwera, wotumizidwa kuchokera kwa Mulungu, wodzozedwa ndi Mulungu, ndi KULANKULA KWA AMBUYE , uthenga ndi mtumiki ali umodzi ndi umodzi.

Ndiye pamene munthu abwera ndi KULANKULA KWA AMBUYE, iye ndi Uthenga ali umodzi.

Kumwamba kumachikamba, Baibulo emachikamba, Uthenga umachikamba, chimodzimodzi.

Mneneri, Mawu, Uthenga; mutumiki, Uthenga, ndi Uthenga, zinali zimozimozi.

Munthu aliyense ndi uthenga wake ndi umodzi.

Kambiranani za Mgodi wa Golide.

Ngati muli ndi Chivumbulutso chilichonse, ndikuganiza kuti amamveketsa bwino; Uthenga ndi mtumiki ali CHIMODZI. Mukumva zomwe ananena…ZOMWEZI!! Ndiye inu simungakhoze kumulekanitsa mtumiki ku Uthenga, atumiki.

Muyenera kuyika MTUMIKI mu mpingo wanu pamodzi ndi UTHENGA umene anabweretsa kapena simukuvomereza UTHENGA WONSE. IWE SIULI MKWATI.

O! Apanso, zimapangitsa Uthenga ndi mutumiki kukhala amodzi. Chakudya chauzimu chakonzeka, ndipo Icho chiri mu nyengo tsopano.

Kwa ife, amene timakhulupirira ntawi ya Mulungu emene ife tikukhalamo, mtumiki yemwe Iye anamutumiza, Mawu aliwonse amene iye analankhula; zinthu izi ndi Chakudya chobisika.

Momwe ife tikukondera Uthenga uwu, ndipo pamene inu mukuganiza, “Pangakhale bwanji wochuluka?” Iye amaika mwala wapamutu pa Iwo potiuza ife yemwe ife tiri tsopano.

Kodi simukuwona ulamuliro wa Mulungu wamoyo mu Mpingo wamoyo, Mkwati? Odwala akuchiritsidwa, akufa aukitsidwa, olumala akuyenda, asaona akuwona, Uthenga ukupita mu mphamvu Yake, pakuti Uthenga ndi mtumiki ali yemweyo. Mawu ali mu Mpingo, mwa munthu.

Mawu amenewo MWA IFE. Ife ndife Uthenga. Ife tiri nawo ulamuliro. Uthenga uwu ndi ife NDI UMODZI!! Lankhulani za kubwebweta mobwerezabwereza.

Mkwati ndi gawo la Mwamuna, Mpingo ndi chimozimozi ndi Khristu. “Ntchito zimene Ine ndichita inunso mudzazichita.”

Ndife gawo la Mwamuna!!

NDIFE CHIMOZIMOZI NDI KHRISTU!!

Inu mukuganiza kuti zikumveka bwino tsopano, ndipo akudalitsa mtima Yanu mukuwerenga mawu awa, yembekezani mpaka inu mumve Liwu la Mulungu likukuwuzani izo kwa inu mulomo ndi khutu Lamlungu lino pa 12:00 p.M., nthawi ya Jeffersonville, pamene ife timva: 65-0718E. Chakudya Chauzimu Panyengo Yoyenera.

Mukuitanidwa kuti mubwere nafe. Ngati simungathe, TYANKANI KULIZA nthawi iliyonse, Uthenga uliwonse, kulikonse, ndipo imvani mtumiki wa Mulungu akukubweretserani Uthenga wa Mulungu.

Bro. Joseph Branham.

Kotero izo ziri lero, kuti Mkate wa Moyo umene ana amadyapo, umatsatira Uthenga wa Mulungu, kuti uwasamalire iwo mu nthawi ya chilala.

Malemba oti muwerenge
1 Mafumu 17:1-7 Amosi 3:7 Yoweli 2:28 Malaki 4:4 Luka 17:30 Yohane 14:12

22-1231 Mpikisano

Uthenga: 62-1231 Mpikisano

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Nkhosa Zam’dera,

Ndikufuna kudzakhalanso ndi Mgonero m’manyumba zathu pa Madzulo a Chaka Chatsopano, pa 31 December. Malangizo momwe mungapezere waini, ndi kuphika mkate wa Mgonero angapezeke m’malinki ali pansi. Linki yomunga daunilode wamawu amtunduwu upezeka posachedwa patsamba lathu. Kapena, munga lize mawu omvera kuchokera pa pulogalamu ya Lifeline.

Kwa anthu akudera la Jeffersonville, munga teng wainivi wa Mgonero pachisanu, Disembala 30, pakati pa 1:00 – 4:00 pm, pansi pa denga la VGR.

Timvera 62-1231 ku Shoshana, kuyambira 5:00 pm EST pa satade, Disembala 31st. M’bale Branham akadzabweretsa Uthenga wa Madzulo wa Chaka Chatsopano, tidzaimilika tepu ndikukhala ndi pafupifupi mphindi 10 za Nyimbo za Kulambira pamene tikukonzekera Mgonero wa Ambuye. tidzayamba anso tepi pamalo pomwe M’bale Branham ayambila utumiki wa Mgonero. Pa tepi iyi, iye wasiya kusambika mapazi gawo la utumiki, chimene ife tizachita.

Pamene tikutembenukira ku chaka china mu Utumiki Wake, tiyeni tiperekenso mwewo yathu kwa Iye mwatsopano kupitira mu kumva Mawu poyamba, ndiye kudya nawo Mgonero Wake. Ndi mwayi wamtengo wapatali bwanji umene tili nawo wokonza nyumba zathu kukhala Malo Opatulika kuti tilandire Mfumu ya Mafumu kuti ibwere kudzatigwirizanitsa ise.

Mulungu akudalitseni,

M’bale Joseph

22-1225 Kuchita Manyazi

Uthenga: 65-0711 Kuchita Manyazi

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mkwati Rebekah,

Atate anatumiza mtumiki wake wokhulupirika, Eliezere, kukasanka Mkwati Wake Rebeka. Ife tamuziba iye, mtumiki Wake wa mngelo wachisanu ndi chiwiri, William Marrion Branham, yemwe Iye anamutuma kuti: Amuyitane, Asonkhanitse, Atsogolere ndipo potsiriza Atidziwitse ife, kwa Iye.

Iye watipatsa ife kutsanulidwa kwakukulu kwa Mphamvu Yake Yofulumizitsa ndipo watifikitsa ife kuziba udindo wathu, malo athu, ndi maudindo athu, pokhala anthu oitanidwa, olekanitsidwa ndi dziko, odzipereka kwa Mulungu. Iye akutitsogolera ndi kutitsogolera mu zinthu zomwe timachita ndi kunena, kubweretsa ulemu ndi ulemerero ku Dzina Lake.

Palibe kanthu, paliponse, kangatilekanitse ife kwa Izo, PALIBE. Ndife otetezedwa Kwamuyayaya mu Ufumu wa Mulungu. Atate watidinda Chidindo Chake ife mpaka kumapeto kwa kopita kwathu.

Satana amatikhonya ISE kuseni ndi usiku. Iye amanena chirichonse kwa ife, ndipo amatitsutsa ife, ndipo amayesa kutipangitsa ife kuganiza kuti ife sitiri Mkwati ameneyo. Amaponya chilichonse m’njira yathu kuyesa kutisokoneza, monga matenda ndi mavuto, koma sitimumvera. Mphamvu yofulumizitsa iyo ili TSOPANO mwa ife ndipo ife tasindikizidwa ndi kukhazikika pa Mawu amenewo. Tikutoloka pa kamelo yathu, kuthamangira kwa Iye popita ku Mgonero wathu waukulu wa Ukwati.

Sitichita manyazi ndi zomwe timakhulupirira; m’malo mwake, ife tikufuna kuti dziko lidziwe, IFE NDIFE ANTHU AMATEPI AMENE AMAKHULUPIRIRA MAWU ONSE OLANKHULIDWA NDI MNENERI WAKE WOKHULUPIRIKA WA ELIEZA yemwe Iye anamutuma kuti akamuitane ndi kutsogolera MKWATI WAKE WA REBEKA. Ife sitimawonjezeranso kapena kuchotsa Mawu AMODZI. Uthenga uwu ndi Mtheradi wathu.

Angakhoze bwanji munthu yemwe ali wodzazidwa ndi Mzimu Woyera, wodzaza ndi Mphamvu ya Mulungu, ndi chikondi cha Mulungu mu mtima mwake, kulankhula kwa munthu maminiti pang’ono chabe ndi kusakamba chinachake cha Uthenga umene iye wangowumva kumene pa Tepi?

Mukakumana ndi anthu amene amadzinenera kuti ndi okhulupirira mu Uthenga wa nthawi yotsiriza ino, mukhoza kuyankhula nawo maminiti pang’ono chabe ndipo mukhoza kudziwa kumene iwo akuyima pa kuliza matepi. Iwo mwina ndi Anthu a Tepi kapena ayi.

Ndi shosaganizila kuti amaona kuti ndi chamanyazi, kapenanso cholakwika, ngati munganene kuti mumaliza matepi kutchalitchi kwanu kapena kunyumba. Iwo amamverera kuti ndi zotsutsana ndi Mawu ndipo osati Njira yoperekedwa ndi Mulungu. Mumaonesedwa pansi chifukwa mumati ndinu “Munthu Watepi”.
[12/24, 12:38 PM] Br moya: Atumiki omwe amaliza matepi m’mipingo yawo amatsutsidwa, ndipo amaitanidwa aulesi. Ndipo ngati inu mumvetsera kwa tepi yomweyo pa nthawi yomweyo, chabwino, sindinu nkomwe mtumiki, ndinu chipembedzo, kapena wopempela munthu.

Ine ndikuganiza anthu onse aja omwe anachita conekiti pa telefoni mu mipingo ndi nyumba zawo, akumvetsera kwa M’bale Branham onse pa nthawi imodzi, iwo ayenera kuti anali achipembedzo nawonso. Ayenera kuti sianali mu pulogalamu la Mulungu. Sanachite manyazi NDIPO NAIFE.

Patawi chabe zochepa mukalankhula ndi anthu, amakudziwitsani pomwepo pomwe ayima: Inde, timadinikiza kuliza. Inde, timamvetsera matepi Lamlungu mu Mpingo kapena nyumba zathu. Inde, tepi yomweyo, na nthawi yomweyo.

Chifukwa chiyani ena amati, “Timapita kutchalitchi Lamlungu m’mawa, Lamlungu usiku, ndi Lachitatu usiku. Tili ndi abusa abwino; Iye amazifotokoza momveka bwino komanso momveka bwino kuti ife timvetse. Iye akufotokoza Uthenga kuti ine ndiwumvetse Iwo. Inu muyenera kukhala ndi utumiki kuti mukhale Mkwati. M’bale Branham sananene kuti mukaziliza matepi mu mpingo.”

Munena chiyani ndiye chofunikira kwambiri? Zomwe alaliki amanena, zomwe M’bale Joseph akunena, kapena zomwe Liwu lomwe la Mulungu likunena pa Tepi? Mtheradi wanu ndi chiyani? Kodi pa Tepi pali chiyani, kapena zomwe wina akunena?

Utumiki ndi wabwino, ndipo mu Mawu. Timawafuna. Koma CHOFUNIKA KWAMBIRI ndi chiyani, kulalikira kapena Matepi?

Ngati Matepi sali chinthu chofunikira kwambiri mu moyo wanu waumuntu, mu moyo wa mpingo wanu, ndiye chinachake chalakwika. Inu mwachoka pa Chifuniro Chabwino cha Mulungu. BWELANI MU NJILA.

Pamene munthu akomana konse ndi Mulungu; osati mu ntchito zina zokhudza maganizo, ziphunzitso za chipembedzo cikhulupililo kapena ciphunziso zozilimbikitsa, koma akafika pa malo monga mmene Mose anacitila. Kumbuyo kwadesati, kuyenda maso ndi maso ndi Mulungu Wamphamvuzonse, ndipo iwe umawona Liwu likulankhula kwa iwe, kosapusana ndi Mawu ndi lonjezo la ntawi, pali chinachake chikuchita kwa iwe! Mwaona, inu simukuchita nawo manyazi Iwo, Iwo amachita chinachake kwa inu.

Masiku atu, chofimba chachikhalidwe chimenecho chang’ambika. Apa payima Lawi la Moto, likuwonetsera Mawu a tsiku lino. Umulungu aphimbidwa mu thupi la munthu. Ulemerero wa Shekinah wa lero. Mulungu ayima ndi kuyankhula pamaso pathu, aphimbidwa mu thupi la munthu.

Mose anali nawo Mawu. Tsopano kumbukirani, Mawu ana wonetseredwa, Mose anali Mose kachiwiri. Mwaona? Koma pamene Mawu amenewo anali mwa iye kuti aperekedwe, iye anali Mulungu; chabwino, iye sanali Mose panonso. Iye anali nawo Mawu a Ambuye a m’badwo umenewo.

Khrisimasi yomwe ife a Rebeka tidzakhala nayo Lamlungu lino. Tsiku lonse, nthawi zosiyanasiyana tsiku lonse. Tidzamva Eliezere wathu akuitana Mkwati wake ndipo tidzakhala tikumuuza kuti sitikuchita manyazi.

Ambuye akupatseni inu Khrisimasi yabwino, yodzazidwa ndi “KUKHALA KWAKE”.

Bro. Joseph Branham

Uthenga: 65-0711 Manyazi

Lemba: Marko 8:34-38

Ndandanda ya Khrisimasi

Okondedwa Abale ndi Alongo,

Chifukwa cha Khrisimasi ili pa mulugu chaka chino, ndamva mumtima mwanga kuti tisakhale ndi nthawi yoti timve Uthenga tsiku limenelo. Mabanja ambiri ali ndi ana ang’ono omwe amasangala kutsegula mphatso zawo m’mawa wa Khrisimasi, ndipo zingakhale zovuta kwa iwo kukhazikika kuti amve Uthenga kapena kuwapangitsa kuti ayembekeze mpaka nthawi ina.

Ndipo, komachabe, pa Khrisimasi, mukudziwa, ana aang’ono, sungawauze mosiyana. Iwo, basi, ndi nthawi ya Khrisimasi kwa iwo. Ndipo iwo siangankale apachikidwe masokosi awo aang’ono, pagankala chinachake. Ndi mwambo, ngakhale mu ziko lathu, kuti iwo amapachika sokosi, ndi chinachake chimzake. Bwanji, ine ndinatero, pamene ine ndinali mwana, ndipo—ndipo ngakhale monga—kutalika kwa Lemba, njira yopunthidwa monga iyo iliri. Koma, ana amamva ana ena akunena kuti, “Chabwino, ndalandira izi pa Khrisimasi. Ndapeza izi.” Ana aang’ono amaima pozungulira, langanani, inu mukudziwa. Inu, inu simungakhoze kuwapangitsa iwo kumvetsa. Mwaona? Chifukwa chake, Khrisimasi inabwela kunkala. Inde.

Pangakale ena omwe angakonde kuwuka kuseniseni ndikumva Uthenga, popeza ali ndi mapulani ndi achibale awo tsiku lomwelo. Choncho ndasankha kuti banja lililonse lisankhe nthawi yomwe ingagwirizane ndi nbanja yawo yomvera Uthenga. Tidzaulutsa Uthenga pa Lifeline katatu kosiyana pa Tsiku la Khrisimasi: 9:00 A.M. – 12:00 PM. – 5:00 P.M.. napapata musaganize kuti muyenera kumvelera imodzi mwa nthawizi, koma sankhani nthawi yabwino kwa inu kapena banja lanu. Chofunikira kwambiri ndichakuti, TYAKANI KULIZA.

Zingawoneke ngati zoseketsa, m’mawa uno, kuvala jasi langa papulatifomu, koma ndinali wokondwa—kusonyeza chikhoto chokongola chomwe chalitchi inandipatsa. Ine ndinamuwona M’bale Neville kuno tsiku lina, anavala suti yabwino iyo, momwe iyo inamukwanira iye koma kwambiri, ndipo ine ndinaganiza, chabwino, ine—ine…izo zinawoneka zabwino kwambiri, ndipo osonkhana akulankhula za izo, ine ninaganiza, “Ine Ndingovala chijasi changa papulatifomu.” Ine basi…

Mukudziwa, ndikulupirira kuti sitikula. Nthawi zonse…Ndipo sindikufuna kukula. Nanga bwanji izo, M’bale Luther? Ayi, sindikufuna kukula. Timafuna kukhalaxhabe ana nthawi zonse.

Ambuye akupatseni inu olide lodabwitsa lodzaza ndi Kukhalapo Kwake.

Bro. Joseph Branham

22-1218 Kodi Mulungu Amasintha Konse Malingaliro Ake Pa Mawu Ake?

Uthenga: 65-0418E Kodi Mulungu Amasintha Konse Malingaliro Ake Pa Mawu Ake?

PDF

BranhamTabernacle.org

Okondedwa A Mesiya,

Ndife odzozedwa a Mulungu; wodzozedwa ndi Mzimu Wake womwewo, mwa ntchito zomwezo, mwa Mphamvu zomwezo, mwa zizindikiro zomwezo. Zachoka ku mphungu kupita ku mphungu, zachoka kumawu kupita kumawu, Mpaka kuzulisisa kwa Yesu Kristu kwaonetsedwa mu thupi lathu lililonse, zakuthupi, zauzimu, kapena zofuna zilizonse zomwe tifuna. Mphamvu yofulumizitsa imeneyo ikukhala ndi kukhala mkati mwathu. Ndife a Mesiya a Mulungu.

Mlungu uliwonse Vumbulutso la Uthenga uwu; yemwe ife tiri, kumene ife tinachokera, ndi kumene ife tikupita,kunkala kwachikulu na chikulu. Ife tikudabwa ndi chiyembekezero chachikulu, Iwo angakhoze bwanji kukhala nawo ulemerero winanso? Zingakhale zomveka mochuluka bwanji? Koma ndi tepi yatsopano iliyonse imene timva, Mulungu amalankhula kwa ife milomo ndi khutu ndi kuwulula zambiri za Mawu Ake kwa ife, ndi kutitsimikizira ife,BAMENE IFE.

Chifunisiso chachikulu cha mtima wa wokhulupirira aliyense ndi kukhala mu CHIFUNIRO CHABWINO CHA MULUNGU. Sitikufuna kukhala mu chifuniro Chake chololera. Mitima yathu ndi yosweka ndipo timasweka ngati tiona kuti tachita chilichonse chimene sichingamusangalatse. Tikudziwa kuti Mulungu ali ndi Chifuniro Chabwino, ndipo tifuna kukhala mu PULOGALAMU YAKE YOFUNILA YOKWANIRI.

Mu moyo wanga, ndapanga kaimidwe kolimba ponena kuti ndikulupirira chinthu chofunikira kwambiri chomwe membala aliyense Mkwati angachite, onse wokunva ndi atumiki chimodzimodzi, bafunika KUTYANKA KULIZA. Ndikulupirira kuti Ndi Liwu LOKHA lotsimikizidwa la Mulungu la Tsiku lathu limene muyenera kumva ndi kukulupilila Mawu aliwonse.

Ine ndanena kuti ndikukhulupirira kuti atumiki ayenera kuti amuyike M’bale Branham mumbuyo mu maguwa awo ndi kuliza matepi mu mipingo yawo, popeza Ilo liri Liwu lofunika kwambiri lomwe anthu ayenera kumva.

Ndakhala ndikutsutsidwa kwambiri mumoyo wanga chifukwa choyimirira pazomwe ndimakhulupirira kuti ndi Pulogalamu Yake ndi Chifuniro Chanbwino. Zakhala zosamvetsetseka ndipo zinanenedwa kuti ine sindimakhulupirira mu atumiki asanu wa Aefeso 4.

Ndanena zambiri, nthawi zambiri zomwe ndi zabodza. Sindinanenepo, kapena kukhulupirirepo zimenezo. Pali ambiri omwe apidamula mawu anga ndikuuza anthu zinthu zomwe sindinanene kapena kuzikhulupirira, koma izi ziyenera kuziyembekezera.

Payenera kukhala Mawu a Baibulo Choonadi. Ngati inu mumadzinenera kuti inu mukukhulupirira Uthenga uwu, ndiye ife tiyenera kutenga zomwe mneneri ananena, popeza Iwo uli kutanthauzira komwe kwa Mawu a Mulungu. Pakuti iye ali wotanthauzira YEKHA wa Mawu amenewo.

Ngati tinafunsa aliyense wa inu, “Ndani akufuna kukhala m’chifuniro Chabwino cha Mulungu?”
Aliyense wa inu anganene kuti, “INDE, ndicho chofunisisa cha mtima wanga.” Chifukwa chake tiyenera kuyang’ana ku zomwe mneneri ananena kuti ndi Chifuniro Chabwino cha Mulungu.

WONANI: Ngati Uthenga wa pa tepi suli Mtheradi wanu, ndipo simukulupirira Mawu aliwonse, IMANI KUWERENGA KALATA IYI. Kwa ine, sindinu wokhulupirira, chifukwa chake si zanu. Ine ndikhoza kokha kukhala ndi zomwe Mulungu ananena pa tepi.

Ife tikufuna zomwe Iye ananena; osati zomwe mpingo unanena, zomwe Dokotala Jones ananena, zomwe winawake ananena. Ife tikufuna zomwe PAKUTI ATERO AMBUYE ananena, zomwe Mawu ananena.

Tiyenera kudzipereka tokha ku chifuniro Chake ndi Mawu Ake. Ife sitiyenera kufunsa Iwo. Ife tiyenera kukulupirira Izo. Osati muyesere kupeza njira yozungulira Izo. Tengani Iwo momwe Iwo aliri.

Ambiri amafuna kuyendayenda ndi kupita njira ina. Ngati mutero, Mulungu adzakudalitsani, koma mukugwira ntchito mu Chifuniro Chake cholekerera, osati mu chifuniro Chake chabwino, Chaumulungu. Mulungu adzakulekani inu kuti muchite chinachake, ndipo ngakhale akudalitseni inu pochichita icho, koma icho sichinali chifuniro Chake Chabwino.

Mulungu anatumiza mngelo wake wachisanu ndi chiwiri ku dziko lapansi kuti aitane Mkwati Wake. Ife tikuupirira kuti Uyo anali Mwana wa Munthu akudziulula Yekha mu thupi la munthu. Ndi Liwu lomwe la Mulungu limene lalembedwa ndi kusungidwa kwa Mkwati Wake.

Mulungu Mwiniwake anamuuza mneneri wake, ngati iwe upangitsa anthu kuti akukhulupirire INU, palibe chimene chidzakuimitseni. Iye anali amene anasankhidwa ndi Mulungu kuti atsogolere Mkwati Wake. Palibe amene angatenge malo ake. Ziribe kanthu kuti AKora angati auke bwanji, kapena a Datani angati, anali William Marrion Branham amene Mulungu anamuitana kuti atsogolere Mkwati Wake. Iyi ndi Pulogalamu la Mulungu ndi CHIFUNIRO Chake CHABWINO.

Ngati anthu sangayende mu chifuniro Chake Chabwino, Iye ali nako chifuniro chongololera Iye akulekani inu kuti muyendemo.

Tsopano, Mulungu ndi wabwino…Iye amatumiza Mawu Ake. Ngati inu simudzawakhulupirira Mawu Ake, ndiye Iye amaika mu Mpingo maudindo asanu osiyana: Choyamba, atumwi, aneneri, aphunzitsi, abusa, alaliki. Iwo ali akukwaniritsa Mpingo.

Motero, utumiki unakwezedwa chifukwa chakuti anthu m’mibadwo yonse sanavomereza PULOGALAMU YA CHIFUNIRO CHABWINO CHA MULUNGU; Mawu Ake olankhulidwa ndi mneneri Wake. Ife tiyenera kukhulupirira Mawu amene mneneri wa Mulungu analankhula. Sitifunikira wina aliyense kapena china chilichonse.

Ndiye ntchito ya atumiki ndi kubweretsa anthu kubwerera ku Pulogalamu la Chifuniro Chake Chabwino, lomwe ndi: KHALANI NDI MATEPI, CHIFUKWA CHILI CHIFUNIRO CHABWINO MULUNGU. Kenako sungani CHIFUNIRO CHABWINO PULOGALAMY patsogolo pawo nthawi zonse ndi: KUTYANKA KULIZA.

Inu muyenera kuti mubwerere ndi kuyamba pamene inu munayambira, kapena pamene inu munasiyira, ndi kutenga Mawu wonse a Mulungu.

Ndiye muyenera kuchita chiyani kuti mukhale mu CHIFUNIRO CHAKE CHABWINO: TYAKANI KULIZA.
Kodi abusa ayenera kuchita chiyani kuti akhale mu CHIFUNIRO CHABWINO CHAKE: TYAKANI KULIZA.

Kodi mneneri wa Mulungu anachita chiyani pamene anapita kumisonkhano? Kupempherera odwala, ndi zinthu monga izo? Iye amakhoza kunena zinthu mozungulira kuti nkhosa zimve izo, chifukwa ife tikudziwa chimene Iye akulankhula. Apo ayi, inali nyambo chabe pa mbedza. Iye anawasonyeza iwo zizindikiro monga kuzindikira za mumtima, ndipo ankadziwa zinsinsi za mitima yawo, kuti azingowakoka anthu. Koma kenako ananena kuti chofunika kwambiri chinali:

Chinthu choyamba chimene mukudziwa, tepi imalowa m’nyumba mwawo. Ndi zimenezo, ndiye. Ngati iye ali nkhosa, iye amabwera nayo pomwepo. Ngati iye ndi mbuzi, amathamangitsa tepiyo.

Ndiwe nkhosa kapena mbuzi? Gulu laling’ono la Mulungu lakhazikika pa Mawu amenewo. Tili mu Chifuniro Chake Chanbwino momwe Tikutyanka kuliza monga izo zinali, ndipo ziri, Pulogalamu Lake loyambirira.

Khalani bwino ndi Mawu Ake, chifukwa ndi zomwe ziti zidzatuluke pamapeto pake, Mawu, Mawu ndi Mawu. “Aliyense amene adzachotse Mawu amodzi kwa Iwo, kapena kuwonjezera liwu limodzi kwa Iwo!” Izo ziyenera kukhala, Mawu amenewo.

Ndine wothokoza kwambiri kwa Ambuye kudziwa, mwa Vumbulutso lauzimu, kuti ine ndiri mu Chifuniro Chake Chabwino molingana ndi Mawu Ake. Ine sindikuwonjezera kutanthauzira kwanga kwa Iwo, kapena kumvetsa kwanga kwa Iwo, koma kumva ndi makutu anga omwe chimene chiri PAKUTI ATERO AMBUYE ndi Chifuniro Chake Chabwino.

Ine ndikukuitanani inu kuti mubwere ndi kudzayendera nafe Lamlungu lino pa 2:00 p.m., nthawi ya Jeffersonville, pamene ife tikumva: Kodi Mulungu Amachinja Maganizo Ake Pa Mawu Ake? 65-0418E. Pali zabwino zambiri mu Uthenga uwu, inu mukhala ACHUMA mu Mzimu Wake Woyera tikamaliza.

Bro. Joseph Branham

Eksodo chaputala 19
Numeri 22:31
Mateyu 28:19
Luka 17:30
Chivumbulutso mutu wa 17

22-1211 Uku Ndi Kutuluka Kwa Dzuwa

Uthenga: 65-0418M Uku Ndi Kutuluka Kwa Dzuwa

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Tempele ya mphamvu,

Munthu wakhala ofunisisa mu mtima mwake kukhala ngati Abrahamu pamene anakhala kunyumba kwake cha m’ma 11:00. Atakweza maso anaona amuna atatu akubwera kwa iye anali nadoti ku zovala zawo. Iye anathamangira kwa iwo mwamsanga, ndipo anati, “Ambuye wanga.” Anayima pamenepo pamaso pake, mu thupi laumunthu akuyankhula, anali Melkizedeki Wamkulu.

Lamlungu lino, kufunisisa mu mitima yathu kudzachitika kwa aliyense wa ife. Ife tonse tidzasonkhana pamodzi kuchokera kuzungulira dziko, kumvetsera kwa Melkizedeki wamkulu yemweyo akuyankhula kwa ISE. Munthu wamene analibe bambo, wopanda mayi, wopanda chiyambi cha masiku kapena mathero a moyo, Mulungu, en morphe, amalankhula nafe kupitila mu milomo ya munthu, momwe Iye anachitira tsiku limenelo kwa Abrahamu.

Palibe njira ina yomvera Liwi pokhapokha kuchila KUTYANKA KULIZA. Sipanayambe pakhala nthawi mu mbiriyakale imene Mkwatibwi wakhala akulumikizidwa kuchokera kuzungulira dziko kuti amve Liwu la Melkizedeki likuyankhula pa nthawi yeniyeni yomweyi. Mulungu akugwirizanitsa Mkwatibwi Wake ndi Liwu limenelo.

Ife takhala nawo, kwa zaka, Mawu a Mulungu. Tsopano ife tiri naye Mulungu wa Mawu, mwaona, ndipo pomwe pano akukhala Mawu Ake. Kodi ndi zoona, chimodzi cha zizindikiro zazikulu zotsiriza zimene zalonjezedwa kwa Mpingo Kudza kwa Ambuye kusanachitike.

Lamlungu lino, Mkwatibwi adzakhala ndi Uthenga wa Isita mu Disemba; ndi Uthenga wake womwe ife titi tiumve.

Zimango. Mphamvu. Mphamvu yofulumizitsa. Khristu woukitsidwa. Anawonetseredwa Ana a Mulungu. Mzimu womwewo umene unakhala mwa Khristu ukhala mwa ife. Moyo womwewo, mphamvu zomwezo, opindula omwewo, omwe Iye anali nawo, ife tiri nawo. Ndemanga yachidule. Mbewu yoyamba imene inafika pa kukhwima ikuweyulidwa pamaso pa anthu. Ife tiri tsopano mnofu wa mnofu Wake, fupa la fupa Lake; Moyo wa Moyo Wake, Mphamvu ya Mphamvu Yake! Ndife Iye!

Yesu Kristu woukitsidwayo; Melkizedeki Mwiniwake, adzafuula ndi kutiuza ife, “Ine ndinali ndi Liwu langa litajambulidwa ndipo linaikidwa pa tepi ya maginito kotero kuti ine ndikhoze kukukokerani inu kwa ine, ndipo ine ndikanakhoza kuyankhula kwa inu monga momwe ine ndinachitira Abrahamu. Ndikufuna kuti mumve kuchokera kwa Ine mwachindunji.”

Inu ndinu Mpingo wanga wokonzedweratu, wokonzedweratu! Matupi anu ndiwo kachisi wa Mphamvu, chifukwa kuyambira pachiyambi inu munali gawo la Zimango.

Ndilo vumbulutso Lauzimu lija la Mawu opangidwa thupi. Ngati Iwo unali thupi mu tsiku limenelo mwa Mwana, Mkwati, Iwo ndi thupi lero mwa Mkwatibwi. Mwaona?

Mphamvu yofulumizitsa imeneyo ikukhala mwa ife. Sitiyenera kuopa kalikonse. Mzimu womwewo umene unali mwa Iye, tsopano uli mwa ife ndipo Iwo ukufulumizitsa thupi lathu lachivundi. Sitikuyembekeza choncho, TIKUDZIWA CHONCHO. Ife tinazipanga izo kale, Iye anatipangira izo.

Ndiye, kutsiriza masanawa, Melkizedeki adzayankhula kachiwiri ndi kunena;

Anthu awa, omwe ali mbadwa anzawo a Ufumu, eni ake a Mphamvu yofulumizitsa, afulumizitseni Izo kwa iwo, Ambuye, pakali pano. Ndipo mulole Mzimu upite kuchokera ku mphungu kupita kwa mphungu, kuchokera ku Mawu kupita ku Mawu, mpaka chidzalo cha Yesu Khristu chiwonetseredwe mu thupi lirilonse, kwa thupi, lauzimu, kapena chosowa chirichonse chimene iwo akuchifuna, pamene ife tikuyika manja athu pa modzi. wina. Mu Dzina la Yesu Khristu.

Kuchokera mphungu kupita kwa mphungu, Mawu kupita ku Mawu, chidzalo cha Yesu Khristu chidzawonetseredwa mu lirilonse la matupi athu. ULEMERERO!!

Izi zikhoza kuchitika kokha ndi KUDINISA KULIZA, kodi bwerani mudzajowine nafe ndi kudzatenga nawo gawo mu chisangalalo chazakudya pa Stored Up Food, pamene tikumva Liwu Lija, Lamlungu pa 12:00 p.m., nthawi ya Jeffersonville, kutibweretsera ife Uthenga, Ndiko Kutuluka Kwake. Dzuba 65-0418M.

Bro. Joseph Branham

Malemba

Levitiko 23:9-11
Mateyu 27:51; 28:18
Marko 16:1-2
Luka 17:30; 24:49
Yohane 5:24; 14:12
Machitidwe 10:49; 19:2
Aroma 8:11
1 Atesalonika 4:16
Ahebri 13:8
Chivumbulutso 1:17-18