All posts by admin5

25-0323 Chisindikizo Chachiwiri

Uthenga: 63-0319 Chisindikizo Chachiwiri

PDF

BranhamTabernacle.org

Okondedwa Omvetsera tepi,

Funso: Kodi tili mu Chifuniro Chake changwiro posewera Matepi?
Yankho: INDE.

Funso: Kodi Mkwatibwi akusowa zambiri kuposa zomwe zanenedwa pa Matepi?
Yankho: AYI.

Funso: Kodi tikuphonya kena kake pomvetsera Matepi OKHA?
Yankho: AYI.

Funso: Kodi tingakhale Mkwatibwi pongomvetsera Matepi OKHA?
Yankho: MOTSINDIKA KWAMBIRI, INDE!

Tsopano kumbukirani, “Palibe choti chiwululidwe; Mulungu sadzachita kanthu, nkonse, mpaka poyamba Iye atawulula icho kwa antchito Ake, aneneri.”

Kotero, ZONSE zomwe Ife tikufuna zinalankhulidwa ndipo ziri pa matepi; kapena, pamene mngelo Wake wachisanu ndi chiwiri adzabwerera kudziko lapansi, IYE adzatiuza ife pamenepo.

O Mkwatibwi, tiyeni tiwone mwamasomphenya zomwe zikuchitika ndi Mkwatibwi wa Khristu padziko lonse lapansi. Atate akusonkhanitsa Mkwatibwi Wake palimodzi ndi Liwu Lake ndipo likubangula, “Pakuti Atero Ambuye.”

Kumbukirani, iye anatiuza chimene Mabingu anali: “Phokoso lowomba lalikulu la Bingu ndi Liwu la Mulungu”. Ndipo kodi Liwu la Mulungu kwa Mkwatibwi ndi chiyani? Mthenga wa mngelo wachisanu ndi chiwiri wa Mulungu, William Marrion Branham.

Iye anati pakubwera Mabingu asanu ndi awiri achinsinsi amene sanalembedwe nkomwe. Ndipo kuti kupyolera mu Mabingu Asanu ndi awiri awo, izo zidzabweretsa Mkwatibwi palimodzi kwa chikhulupiriro chokwatulitsa.

Mawu a Ambuye amadza kwa aneneri Ake. Ngati Iye akanakhala ndi kachitidwe kabwinoko, Iye akadagwiritsa ntchito iko. Iye anasankha dongosolo labwino kwambiri pachiyambi ndipo Iye sangasinthe, ndipo sadzasintha.

Chotero, Liwu la Mulungu, likuyankhula kupyolera mwa mngelo Wake wachisanu ndi chiwiri, likubweretsa Mkwatibwi Wake palimodzi ndi kutipatsa ife Chikhulupiriro Chokwatulitsa.

Mpingo sunadabwepo kuchokera 1933, kumusi ku mtsinje tsiku lija, kuti William Marrion Branham ndi Liwu la Mulungu, Likubangula, “Pakuti Atero Ambuye,” ndipo anatumizidwa kuyitana, kusonkhanitsa, ndi kutsogolera Mkwatibwi.

Ine ndikufuna kuti ndikuyitaneni inu kuti mubwere kudzamvetsera nafe Lamlungu pa 12:00 p.m., nthawi yaku Jeffersonville, pamene Ambuye wathu Yesu akutsegula Bukhu, akumatula Chisindikizo, ndi kuchitumiza Icho ku dziko lapansi, kwa mngelo Wake wachisanu ndi chiwiri, kuti adzawululire Icho kwa Ife!

M’bale. Joseph Branham

Tsiku: Lamlungu, pa 23 Marichi , 2025
Uthenga: Chisindikizo Chachiwiri 63-0319
Nthawi: 12:00 PM, nthawi yaku Jeffersonville

Malemba oti muwerenge musayambe kumvera Uthenga:
Mateyu woyera 4:8 / 11:25-26 / 24:6
Marko woyera 16:16
Yohane woyera 14:12
2 Atesalonika 2:3
Ahebri 4:12
Chibvumbulutso 2:6/6:3-4/17/19:11-16
Yoweli 2:25
Amosi 3:6-7

25-0316 Chisindikizo Choyamba

Uthenga: 63-0318 Chisindikizo Choyamba

PDF

BranhamTabernacle.org

Okondedwa Wanga Mfumukazi ya Kumwamba,

Ine Ndili nazo zochuruka za inu munkhokwe Lamlungu lino. Choyamba, mudzamva kugunda kwa Bingu.  Ilo lidzakhala Liwu Langa, Liwu la Mulungu kuyankhula kwa inu, Mkwatibwi Wanga. Ndidzakhala ndikuwululira Mawu Anga kwa inu kuposa kale. Inu mudzandiwona Ine, Mwanawankhosa wamagazi amene anaphedwa kuchokera ku maziko a dziko, akutenga ndi kutsegula Bukhu, kumatula Zisindikizo, ndi kulitumiza Ilo kumusi uko ku dziko lapansi, kwa m’thenga Wanga wa mngelo wachisanu ndi chiwiri, William Marrion Branham, kuti adzawululire kwa INU zinsinsi zimene zakhala ziri zobisika kuchokera ku maziko a dziko!

Kudzakhala kukuwa, kufuula, ndi ma aleluya ochokera kuzungulira dziko lonse pamene ine ndikuyankhula kwa inu. Mkango udzakhala ukubangula; odzozedwa, mphamvu, ulemerero, mawonetseredwe adzakhala oposera mawu. Inu, Mfumukazi Yanga, mudzakhala pamodzi m’malo amwambamwamba pamene Ine ndikulankhula ndi inu ndi kukupatsani inu mphavu ya Chikhulupiriro yokwatulitsa. Ife

Kumbukirani, inu muyenera kukhala nacho Chikhulupiriro chija chimene chinaperekedwa kamodzi kwa oyera. Ndinakuuzani kuti, Muzimvera mngelo wanga amene ndinamutuma kwa inu.

Iye ali woti “abwezeretse Chikhulupiriro cha ana kubwerera kwa atate.” Chikhulupiriro choyambirira cha Baibulo ndi chakuti chibwezeretsedwe ndi mngelo wachisanu ndi chiwiri.

Mawu Anga amakuuzani inu, mu masiku a Liwu la mngelo wachisanu ndi chiwiri, kuwomba kwake, kuwomba lipenga la Uthenga; ayenera kutsiriza zinsinsi zonse za Mulungu. Sipangakhoze kukhala chinthu chimodzi chowonjezedwako ndipo palibe chochotsedwapo kwa chimene ine ndinanena pa matepi; muzingonena zomwe ndidalankhula kudzera mwa m’thenga Wanga wa m’ngelo. Ichi ndichifukwa chake ndinali nalo ilo lidajambulidwa, kuti mophweka muzingotha ​​KUSINDIKIZA KULISEWERA ndikumva ndendende zomwe ndinanena, ndi momwe Ine ndinazinenera. Idzakupatsani Inu mphavu ya Chikhulupiriro chokwatulitsa.

Mfumukazi yanga yokondedwa, m’maso mwanga inu muli wangwiro, mtheradi, wopanda uchimo pamaso panga. Osadandaula, Inu SIMUDZAPITA mu chisautso; pakuti mwalandira Magazi Anga, Mawu Anga, mngelo Wanga, Liwu Langa, kotero inu kwenikweni mulibe uchimo pamaso panga.

Ine Ndilinazo Izo zainu zazikulu munkhokwe. Inu mukuwona Mawu Anga akufutukuka pamaso panu tsiku lililonse. Ndakhala ndikuyika zizindikiro kumwamba kuti ndikuuzeni kuti chinachake chikukonzekera kuchitika. Ine Ndikubwera, khalani okonzekera. Ikani Mawu Anga, Liwu Langa, choyamba m’moyo wanu.

Ikani chirichonse pambali, palibe chinthu chofunika kwambiri kuposa Mawu Anga. Ndikudziwa kuti m’dani akufuna kukugwetsani, koma ndinakulonjezani kuti ndidzakukwezani. Ine ndiri ndi inu, ngakhale MWA INU. Inu ndi Ine tikukhala Amodzi pamene Ine ndikuwululira Mawu Anga kwa inu.
Inu mukudziwa mu mtima mwanu, NDINU Mfumukazi Mkwatibwi wanga. Inu mukudziwa ine ndinakukonzeranitu inu. MUkudziwa kuti ndimakukondani. Mukudziwa kuti ndimakhala nanu mphindi iliyonse ya tsiku lililonse. Inu mukudziwa kuti Ine SINDIDZAKUSIYANI INU.

Tizikhala ndi nthawi yodabwitsa yotere pamene ndikukuwululirani zambiri Lamlungu lililonse, tsiku lililonse, pamene mukundimva Ine ndikulankhula kudzera mwa mngelo Wanga kwa inu. Ena mwina sangamvetse kapena kuwona zomwe inu mukuwona, koma Izo zazikika mu mtima mwanu kuti iyi ndi Njira Yanga yoperekedwa.

Ndi pothawirapo bwanji ndakupatsani inu. Inu mophweka Mutha Kungosindikiza kuSewera nthawi ina iliyonse, masana kapena usiku, ndikundimva ine Ndikulankhula nanu. Ndidzabweretsa chitonthozo ku moyo wanu pamene ndikuwululira Mawu Anga ndikukuuzani inu yemwe inu muli. Uthenga uliwonse ndi wa Inu, ndipo wa inu nokha. Tikhoza kuyanjana ndi kupembedza limodzi nthawi iliyonse yomwe inu mukufuna.

Lamlungu pa 12:00 P.M., nthawi ya ku Jeffersonville, gawo la Mkwatibwi lidzasonkhanitsidwa kuchokera kuzungulira dziko kuti adzamve zinsinsi zazikulu izi zikuwululidwa. Ine Ndikukuitanani inu kuti mubwere kulumikizana nafe pomwe tikumvera, 63-0318 – “Chisindikizo Choyamba”.

M’bale. Joseph

Malemba oti muwerenge pokonzekera kumva Uthenga:
Mateyu 10:1 / 11:1-14 / 24:6 / 28:19
Yohane 12:23-28
Machitidwe 2:38
2 Atesalonika 2:3-12
Ahebri 4:12
Chivumbulutso 6:1-2 / 10:1-7 / 12:7-9 / 13:16 / 19:11-16
Malaki chaputala chachitatu ndi chaputala cha folo
Daniele 8:23-25/11:21/9:25-27

25-0309 Cholekanitsa Pakati Pa Mibadwo Isanu Ndi Iwiri Ya Mpingo Ndi Zisindikizo Zisanu Ndi Ziwiri

Uthenga: 63-0317E Cholekanitsa Pakati Pa Mibadwo Isanu Ndi Iwiri Ya Mpingo Ndi Zisindikizo Zisanu Ndi Ziwiri

PDF

BranhamTabernacle.org

Okondedwa Iwo Obwezeretsedwa,

Ine Sinditopa kumva Liwu la Mulungu likutiuza kuti ndife ndani, komwe timachokera, komwe tikupita, zomwe tili.
wolandira cholowa, ndi momwe amatikondera ife.

unsembe wauzimu, fuko lachifumu, kupereka nsembe zauzimu kwa Mulungu, zipatso za milomo yawo, kupereka mayamiko kwa Dzina Lake.” Ndi a—ndi anthu otani! Iye ali nawo iwo.

Chitonthozo chathu chokha ndi mtendere zimadza pakumva Liwu la Mulungu likulankhula kwa ife, ndiye kulankhula mobwezera kwa Atate mwa kupereka nsembe zauzimu mwa zipatso za milomo yathu, kupereka matamando ku Dzina Lake.

Dziko lonseli likubuula. Chirengedwe chikubuula. Ife tikubuula ndi kuyembekezera kudza kwa Ambuye. Dzikoli lilibe kanthu kwa ife. Ife tiri okonzeka kuti tichoke ndi kupita ku Mgonero wathu wa Chikwati ndi Kwathu Kwamtsogolo limodzi ndi Iye ndi onse amene ali Kumeneko, basi kupyola katani ya nthawi, akutiyembekezera ife.

Tiyeni tidzuke tidzigwedeze tokha! Tsinani chikumbumtima chathu, tidzidzutse tokha ku zomwe zikuchitika pakali pano ndi zomwe zidzachitike mu mphindi ya kuphethira kwa diso.

Palibe mu mbiriyakale ya dziko zomwe zakhala zotheka kuti Mkwatibwi wa Khristu akhale wolumikizana kuchokera kuzungulira dziko, onse pa nthawi yofanana yomweyo, kuti amve Liwu la Mulungu likuyankhula ndi kuwulula Mawu Ake kwa Mkwatibwi Wake.

Okhulupirira, dzifunseni nokha, ndi liwu liti, mtumiki wuti, munthu uti, angalumikizitse ndi kubweretsa Mkwatibwi wa Khristu pamodzi? Ngati inu muli Mkwatibwi wa Khristu, inu mukudziwa kuti palibenso Liwu lina koma Liwu la Mulungu pa matepi.

Inde, Mzimu Woyera uli mwa aliyense wa ife, mu udindo uliwonse wa mpingo, koma Mulungu Mwiniwake anatiuza ife kuti Iye adzaweruza dziko ndi Mawu Ake. Mkwatibwi amadziwa kuti Mawu Ake amabwera kwa mneneri Wake. Mneneri wake ndi YEKHAYO wotanthauzira Wauzimu wa Mawu Ake. Zimene Iye analankhula sizingawonjezedwepo kapena kuchotsedwapo. Ndi Mawu,a pa matepi, amene ife tonse tidzaweruzidwa nawo, ndipo palibe mawu ena kapena kutanthauzira kwa Mawu amenewo.

Sizingatheke kuti liwu lina lirilonse ligwirizanitse Mkwatibwi. Ndi Liwu la Mulungu lokha pa matepi lingakhoze kugwirizanitsa Mkwatibwi Wake. Ndi Mawu okhawo omwe Mkwatibwi angagwirizane nawo. Ndi Liwu lokhalo limene Mulungu Mwiniwake anatsimikizira kukhala Liwu Lake kwa Mkwatibwi Wake. Mkwatibwi Wake ayenera kukhala mu Malingaliro Amodzi ndi Chigwirizano Chimodzi kuti akhale ndi Iye.

Ma tumiki akhoza kutumikira, aphunzitsi akhoza kuphunzitsa, azibusa akhoza kuchitira ubusa, koma Liwu la Mulungu pa matepi liyenera kukhala Liwu lofunika kwambiri lomwe iwo ayenera kuliyika pamaso pa anthu. Iwo ndiwo Mtheradi wa Mkwatibwi.

Ngati muli ndi Vumbulutso la izo, ndiye ichi ndi chimene chiti chichitike.

Mawu amatiuza ife kuti Adamu anataya cholowa chake, dziko lapansi. Tsopano, ilo linachoka mdzanja lake kupita kwa iye amene anamugulitsa, Satana. Iye anagulitsa chikhulupiriro chake mwa Mulungu, kwa malingaliro a Satana. ndipo iye analanditsa chidutswa chirichonse kwa manja a Satana. Iye anachipereka icho kuchokera mdzanja lake kupita kwa Satana.

Mulungu ndi Mulungu wa chilengedwe chonse, kulikonse, koma Mwana Wake, Adamu, anali ndi dziko lapansi ili pansi pa ulamuliro wake. Iye amakhoza kuyankhula, iye amakhoza kutcha dzina, iye amakhoza kunena, iye amakhoza kuimitsa chirengedwe, iye ankakhoza kuchita chirichonse chimene iye ankafuna kutero. Iye anali ndi ulamuliro wathunthu, wapamwamba kwambiri padziko lapansi.

Adamu anataya zonse, koma ulemerero kwa Mulungu, zonse zomwe iye anataya ndi kulandidwa zidawomboledwa ndi Muomboli wathu Wachibale, palibe wina koma Mulungu Wamphamvuzonse, amene anakhala Emanuele, mmodzi wa ife. TSOPANO, NDI ZATHU.

Ndife ana Ake aamuna ndi aakazi amene ati adzalamulire ndi kukhala mafumu ndi ansembe limodzi ndi Iye. Tili ndi moyo wosatha ndi Iye ndi onse amene timawakonda. Sipadzakhalanso matenda, sipadzakhalanso chisoni, sipadzakhalanso imfa, umuyaya basi zonse palimodzi.

Tikaganizira zimenezi, tingalole bwanji kuti mdierekezi atigwetse pansi? Ndi ATHU, ndikomwe tikupita posachedwa. Iye watipatsa ife chinthu chachikulu kwambiri chimene angatipatse ife. Masiku ochepa awa a mayeso ndi mayesero padziko lapansi amizidwa mwachangu ndi KUGONJETSA KWATHU KWAKUKULU MASIKU CHABE OMWE ALI PA TSOGOLO PATHU.

CHIKHULUPIRIRO chathu sichinakhale chokulirapo. Chisangalalo chathu sichinakhalepo chachikulu. Timadziwa kuti ndife ndani komanso komwe tikupita. Tikudziwa kuti tili mu chifuniro Chake changwiro pa kukhala ndi Mawu Ake. Chomwe ife tikusowa kuti tichite ndi kukhala nawo matepi ndi kukhulupirira Mawu aliwonse; osati kuvetsa zonse, KOMA KUKHULUPILIRA MAWU ONSE…ndipo TIMAWACHITA!

Chikhulupiriro chimadza pakumva, kumva Mawu. Mawu amadza kwa mneneri. Mulungu analankhula Izo. Mulungu anazijambula Izo. Mulungu anaulula Izo. Ife tikuzimva Izo. Ife timakhulupirira IZO.

Inu mukhoza kupeza Vumbulutso ili kokha pa kumva Liwu la Mulungu pa matepi.

Zonse izo zimene Khristu ati adzachite pa matsiriziro zidzaululidwa kwa ife sabata ino, mu Zisindikizo Zisanu ndi ziwiri, ngati Mulungu angatilole ife. Mwaona? Chabwino. Izo zidzaululidwa. Ndi kuululidwa, pamene Zisindikizo zikutsegulidwa ndi kuperekedwa kwa ife, ndiye ife tikhoza kuona chimene dongosolo lopambana la chiombolo ili liri, ndipo liti ndi momwe chiti chidzachitike. Zonsezo ndi zobisika mu Bukhu ili la chinsinsi pano. Ndi losindikizidwa, liri ndi Zisindikizo Zisanu ndi ziwiri, ndipo kotero Mwanawankhosa ndi yekhayo Mmodzi Amene angamatule izo.

Lamlungu lino pa 12:00 P.M., nthawi yaku Jeffersonville, gawo la Mkwatibwi kuchokera kuzungulira dziko lapansi adzakhala akumvetsera ku Liwu la Mulungu onse pa nthawi imodzi. Tidzakhala tikugunda mwamphavu kumwamba ndi mapemphero athu ndi kumulambira IYE. Ndikukuitanani Inu kuti mubwere kulumikizana nafe pamene tikumva: Cholekanitsa Pakati Pa Mibadwo Isanu Ndi lwiri Ya Mpingo Ndi Zisindikizo Zisanu Ndi Ziwiri 63-0317E.

Chonde musaiwale za kusintha kwa nthawi yaku Jeffersonville kumapeto a sabata ino.

M’bale. Joseph Branham

25-0302 Mulungu Kudzibisa Yekha Mu Kuphweka, Ndiye Nkudziwulula Yekha Momwemo

Uthenga: 63-0317M Mulungu Kudzibisa Yekha Mu Kuphweka, Ndiye Nkudziwulula Yekha Momwemo

PDF

BranhamTabernacle.org

Okondedwa Akakombo Apadziwe

Pa February 28, 1963, Kunagunda. Whii-Whii, Angelo Asanu ndi awiri anabwera kuchokera ku Umuyaya ndipo anawonekera kwa Mngelo Wachisanu ndi chiwiri wa Mngelo Mthenga wa Mulungu. Iye anakwatulidwira mmwamba mu piramidi ya kuwundana. Kenako, mtambo wauzimu unawonekera mu mlengalenga ku Arizona. Icho chinali chizindikiro, Mulungu anali kutumiza mngelo Wake wachisanu ndi chiwiri kubwerera ku Jeffersonville kuti adzatsegule Zisindikizo Zisanu ndi ziwiri.

February 28, 2025, mapulaneti asanu ndi awiri amayenda mlengalenga. Mkwatibwi akudzikonzekeretsa Yekha kuti kudzasonkhana ndi kumva Zisindikizo Zisanu ndi ziwiri.

Inu mukuitanidwa, ndi Ambuye Mwiniwake, kuti mudzasonkhane ndi Mkwatibwi kuchokera kuzungulira dziko, kuti mudzamve Liwu la Mulungu likuwulura Chivumbulutso cha Zisindikizo Zisanu ndi ziwiri.

Tsiku limene aneneri ndi anzeru ankalilakalaka ndi kuliyembekezera kuyambira pa chiyambi cha nthawi, likuchitika. Mngelo wamphamvu amene Mulungu ananena kuti adzatumiza padziko lapansi m’masiku otsiriza wabwera kudzatsegula ndi kuwulula zinsinsi zobisika za Mulungu, kuti Ambuye wathu Yesu abwere chifukwa cha Mkwatibwi wake wokhulupirika ndi kutitengera Ife ku Mgonero wathu wa Ukwati.

Ntchito yanga yoyamba, mmene ine ndimalowa mkachisi watsopano, ine ndimakwatitsa mnyamata ndi msungwana atayima mu ofesi. Icho chikhale choyimira, kuti ine ndidzakhala mtumiki wokhulupirika kwa Khristu, kuti ndipeze Mkwatibwi wokonzekera mwambo wa Tsiku limenelo.

Lero , Mawu awa akukwaniritsidwa. Mulungu akuyankhula kupyolera mwa mngelo Wake, kukonzekeretsa Mkwatibwi Wake ku mwambo wa Tsiku limenelo. Tikutsatira malangizo kudzera mu kalata. Mkwatibwi wadzikonzekeretsa Yekha pa KUKHALA NDI MAWU A MULUNGU PA MATEPI.

Kodi tangomva zotani m’maloto ndi masomphenya? Chakudya, NDI ICHI APA, awa ndi malo. Liwu linati kwa iye, “Liwu linanena kwa ine, “Liwu linanena kwa ine, “Bweretsa mkati Chakudya. Uchisunge Icho mkati. Iyo ndi njira yokha yowasungira iwo pano, ndi kuwapatsa iwo Chakudya.”

Ambiri amakhulupirira kuti iye akungotanthauza, “ingokhalani ndi Mawu,” ndipo izo nzowonadi, iye akunena kuti; koma Mkwatibwi adzawerenganso pakati pa mizere pamene Mkwati akuyankhula kwa Mkwatibwi Wake.

Ngakhale masomphenya amene Mulungu amapereka pa malo ano, iwo ali osamvetsedwa kwambiri. Ndicho chifukwa inu mukundimva ine pa matepi, kuti, “Nenani zimene matepi akunena. Nenani zimene masomphenya akunena.” Tsopano, ngati inu muli maso kwambiri, inu muona chinthu china. Mwaona? Ine ndikuyembekeza kuti ine sindikusowa kuchigwira icho mdzanja langa ndi kukuonetsani inu.

Ngakhale masomphenyawo sanamvetsetsedwe, ngakhale kuti anali atatha kale kupereka matanthauzo kwa iwo. Ndi zomwe amatiuza, ngati simukufuna kusokonezedwa, kapena kusamvetsetsa, Dinani Sewerani kuti mumve ndendende zomwe Liwu la Mulungu likunena.

Ine ndikudziwa kuti Mawu ali ndi matanthauzo apawiri, koma uku ndi kumasulira kwanga: Maloto ndi masomphenya onse ananena chinthu chomwecho; khalani nawo matepi. Ngati inu muli ndi funso, pitani ku matepi. Matepiwo ndi Chakudya chosungidwa-cha Mulungu. Ingonenani zomwe zili pa matepi; musati muwonjezere kalikonse kwa Iwo. Matepi ali PAKUTI ATERO AMBUYE kwa Mkwatibwi. Mawu amadza kwa mneneri, yekha. Mneneri ndi YEKHA wotanthauzira Wauzimu wa Mawu. Mneneri anali woti ayitane ndi kutsogolera Mkwatibwi. Ine ndidzaweruzidwa ndi zomwe zinanenedwa pa MATEPI.

Chilichonse chimandilozera ine ku MATEPI.

Okondedwa anga Akakombo apadziwe, kwa ine, KUSINDIKIZA KUSEWERA NDI MULUNGU MU KUPEKWA KWA LERO.

Mlungu uliwonse ndimakhala osangalala kwambiri; ndi chiyani chiti chidzaululidwe lero pamene Mkwatibwi Wake adzasonkhana kuti amve Uthenga? Ine Ndikudziwa kuti Mzimu Woyera adzakhala akudzoza aliyense wa ife pamene akuwululira Mawu Ake kuposa kale. Ine ndikumverera, pa mphindi iliyonse, Iye adzabwera ndi kudzatitengera ife ku Mgonero wathu wa Chikwati.

Ife tiri, ana aamuna ndi aakazi a Mulungu. Ife Tili, mphukira zochokera kwa Mulungu. Ife ndicholowa cha dziko lapansi. Ife tikhoza kulamulira chilengedwe. Ife tikhoza kulankhula nkukhalapo. Ndife Mkwatibwi!

Tiyeni tidzipereke tokha mwatsopano ku ntchito, ndi kudzipatulira tokha kwa Khristu.

M’bale. Joseph Branham

Tsiku: Lamlungu, Marichi 2, 2025
Uthenga: Mulungu Kudzibisa Yekha Mu Kuphweka, Ndiye Nkudziwulula Yekha Momwemo
63-0317M
Nthawi: 12:00 PM, nthawi yaku Jeffersonville.

25-0223 Kodi Ichi Ndi Chizindikiro Cha Mapeto, Bwana?

Uthenga: 62-1230E Kodi Ichi Ndi Chizindikiro Cha Mapeto, Bwana?

PDF

BranhamTabernacle.org

Okondedwa Mabwana,

Ichi ndi Chizindikiro. Iyi ndi nthawi. Uwu ndi, Uthenga. Awa ndi Mawu. Ili ndilo, Liwu la Mulungu. Uyu ndi Mwana wa Munthu. Iyi ndiyo, njira yoperekedwa ndi Mulungu. Awa ndiwo mapeto a nthawi.

Palibe m’neneri, palibe mtumwi, palibe, mu nthawi iliyonse, anayamba wakhalapo mu nthawi yotero yomwe ife tikukhalamo tsopano. Zalembedwa m’miyamba. Zalembedwa pa nkhope ya dziko lapansi. Zalembedwa m’nyuzipepala iliyonse. Awa ndiwo mapeto, ngati mungathe kuwerenga zolembedwa.

Iye amene ali nalo khutu, muloleni iye amve zomwe Mulungu anayankhula, ndi kuchita rekodi, kotero iwo sakanakhala mawu anga, maganizo anga, lingaliro langa, koma Liwu lomwe la Mulungu likulangiza Mkwatibwi Wake chimene chiri njira Yake YOKHA yangwiro yoperekedwa kwa lero.

Bwerani ndi kumvetsera pamene Iye akutiuza ndi kuwulula kwa ife mwa malembo, mwa masomphenya, mwa kutanthauzira kwa maloto, kuti tikhale ndi Uthenga, kuti tikhale ndi matepi. Muzinena ZOKHAZO zomwe zili pa matepi.

Palibe njira yabwino, kapena njira yotsimikizika, yoposa kumva Liwu la Mulungu kuchokera kwa Mulungu Mwiniwake. Mulungu analamulira Mkwatibwi Wake polankhula kupyolera mwa mneneri Wake ndi kutiuza ife, KUSINDIKIZA KUSEWERA, munyengo.

Lankhulani Ilo, lilalikireni ilo, chitirani umboni za ilo, ndi kuliwuza dziko lapansi za ilo, koma Iye amatiuza ife kuti pali njira imodzi yokha yangwiro yoperekedwa kuti afikitse Mkwatibwi ungwiro: kumvetsera kwa Liwu la Mulungu pa matepi. Ngati chinachake chikukudodometsani inu, sewerani tepiyo. Iyenera kukhala YOYAMBA, ndipo ndilo Liwu lofunika kwambiri lomwe muyenera kulimva. Ndi Mawu Ake angwiro amene anawayika pa tepi.

Tsopano fanizirani ngakhale ilo ndi enawo, maloto. Awa anali masomphenya. Chakudya, ndi Ichi apa. Awa ndiwo malowo.

Mvetserani, mwa maloto ndi masomphenya, Chakudya cha Mkwatibwi chiri kuti? Malowo ali kuti? Uthenga wa Mkwatibwi uli pa matepi.

Ndipo pano ndimamverera ngati kwathu, kwa ine. Malo ake ndi ano. Ndipo ngati inu mungazindikire, maloto anayankhula chinthu chomwecho, onani, kumene Chakudya.

Kuti atsimikizire kuti ife tiri nacho Icho, iye akutiuza ife kamodzinso, matepiwo ali Chakudya cha Mkwatibwi.

“Palibenso nthawi.” Ngati iyo ili, tiyeni tidzikonzekere tokha, abwenzi, kukakomana naye Mulungu wathu.

Inde, Ambuye, ndicho chokhumba cha mtima wathu, kukonzekera kukumana nanu, kuti ife tikhale Mkwatibwi Wanu. Tichite chiyani Ife Ambuye? Njira Yanu yoperekedwa ndi yotani? Dongolo lanu ndilotani? Njira Yanu yangwiro ndi iti? Inu munatitumizira ife mneneri yemwe Inu mudakhoza kuyankhula naye kuti atiuze ife. Chonde tilangizeni.

Pakhala pali Chakudya chochuluka chimene chayikidwa muno tsopano. Tiyeni tichigwiritse ntchito Icho. Tiyeni tichigwiritse ntchito Icho tsopano.

Kodi munthu angakhale wakhungu bwanji? Iye Amatiuza choti tichite: pa matepi pali chakudya chambiri chosungidwa; chigwiritseni ntchito TSOPANO. Ili ndi langizo la Mulungu kwa Mkwatibwi Wake.

Ngati inu mukuti inu mumakhulupirira Uthenga uwu, khulupirirani William Marrion Branham ndi mneneri wamthenga wa Mulungu wotumidwa kudzayitana Mkwatibwi; moyo wake umakwaniritsa malembo Onse omwe ananena za iye; khulupirirani ilo kuti ndi Liwu la Mulungu la tsiku lino, Kotero IYE; Mulungu, akuyankhula kupyolera mwa mneneri Wake, amamuuza Mkwatibwi mu Chichewa chomveka bwino choti achite.

Ngakhale kuti ife timasekedwa, kuzunzidwa, ndi kunyozedwa chifukwa choti ife timangomvetsera ku matepi, ife tikuchita ndendende zomwe Iye anatiuza ife kuti tichite. Zikomo Ambuye chifukwa cha Vumbulutso.

Ndikufuna kuitana dziko kuti mulumikizane nafe Lamlungu lino nthawi ya 12:00 p.m., nthawi ya ku Jeffersonville, monga tikumva: 62-1230e, “Kodi Ichi Ndi Chizindikiro Cha Mapeto, Bwana?” Tidzakhala tikumva zonse za izo :

Mabingu, Zisindikizo Zisanu ndi ziwiri, Thanthwe la Piramidi, Chakudya Chauzimu, Muyaya, Kuwundana kwa Angelo, Likulu Langa, Masomphenya, Maloto, Uneneri, Zinsinsi Zobisika, Lemba pambuyo pa Lemba.

Palibe chinthu china chachikulu m’moyo uno kuposa kumva ndi kumvera Liwu la Mulungu.

M’bale. Joseph Branham

Malemba:
Malaki Chaputala 4
— Mateyu 13:3-50
Aroma 9:33; 11:25; 16:25
1 Akorinto 14:8/15 Mutu
Agalatiya 2:20
Aefeso 3:1-11 / 6:19/ 5:28-32
Akolose 4:3
1 Atesalonika 4:14-17
1 Timoteo 3:16
Ahebri 13:8
2 Petulo 2:6
Chivumbulutso 1:20 / 3:14 / 5:1 / 6:1 / 10:1-7 / 17th Chapter

25-0216 Sabata La Makumi Asanu Ndi Chiwiri La Daniele

Uthenga: 61-0806 Sabata La Makumi Asanu Ndi Chiwiri La Daniele

PDF

BranhamTabernacle.org

Okondedwa Iwo Akuyang’anira Ndinso Akuyembekenzera,

Pali chisangalalo pakati pa Mkwatibwi kuposa kale. Tili pa kuyembekezera kwakukulu; Chaka chathu chachisangalalo chikukonzekera kuti chichitike. Mkwatibwi wayembekezera motalika kwambiri kuti tsiku ili lifike. Mapeto a nyengo ya m’badwo wa Amitundu yafika ndipo chiyambi cha muyaya ndi Ambuye wathu chiyamba posachedwapa.

Ife tikumvetsa nthawi yomwe tikukhalamo pa kumva Mawu. Nthawi yatha. Nthawi ya Mkwatulo yayandikira. Tafika. Mzimu Woyera wabwera ndi kuwulula kwa Mkwatibwi Wake zinthu zonse zazikulu, zakuya, zinthu za zinsisi.

Ife tiri mu kusimidwa, kufunafuna Mulungu; kudzikonzekeretsa tokha. Tataya zinthu zonse za dziko lino. Zosamalira za moyo uno sizitanthauza kanthu kwa ife. Chikhulupiriro chathu chafika patali kwambiri kuposa kale lonse. Mzimu Woyera ukumupatsa Dona Wake wosankhidwa Chikhulupiriro chokwatulitsa, kotero Iye akhoze kubwera ndi kumuchotsa Iye.

191 Masabata sikisite naini awa analondolera mwangwiro; kupita kwina kwa Ayuda kumalondolera mwangwiro; m’badwo wa mpingo umalondolera mwangwiro. Ife tiri pa mapeto a nthawi, nthawi yotsiriza, m’badwo wa mpingo wa Laodikaya, kutha kwa iwo. Atumiki nyenyezi onse alalikira uthenga wawo. Iwo wapita kunja. Ife tikungogubuduka.

Ndi nthawi yodabwitsa bwanji yomwe Ife tikukhalamo. Ndi nthawi yovuta kwambiri pamene m’dani akulimbana ndi aliyense kuposa kale. Iye akuponya zonse zimene ali nazo kwa ife. Iye ali mu kusimidwa, chifukwa akudziwa kuti nthawi yake yafika kumapeto.

Koma panthawi yomweyomweyo, Ife sitinakhalepo osangalala kwambiri mmiyoyo yathu.

• Sitinakhalepo pafupi ndi Ambuye.
• Mzimu Woyera amadzaza mum’tsempha uliwonse wa thupi lathu.
• Chikondi chathu pa Mau ake sichinakhale chokulirapo.
• Vumbulutso lathu la Mau ake limadzaza moyo wathu.
• Tikugonjetsa mdani aliyense ndi Mau.

NDIPO, sitinakhalepo otsimikiza kwambiri kuti ndife ndani:

• OKONZEDWERATU
• OSANKHIDWA
• OSANKHIDWA
• Mbewu Yachifumu
• OKOMA APA MTIMA
• AMUYAYA, IWO OVALA MWINJIRO WOYERA, MAYI JÉZU, OMVETSERA KU MATEPI, OWUNIKILIKIDWA, NAMWALI WOLANGIDWA, WODZAZIDWA NDI MZIMU, WOSAGONJETSEDWA, WOKHAZIKITSIDWA KWAUZIMU, WOSAIPITSIDWA, MKWATIBWI WA MAWU NAMWALI.

Mchiyani Chikubwera chotsatira ? Mwala ukubwera. Tikuyang’ana, kuyembekenzera ndi kupemphera mphindi iliyonse tsiku lililonse. Palibenso china chilichonse chovuta koma kudzikonzekeretsa tokha pa kubwera kwake.

Sikuti, “Tikuyembekeza choncho”, TIKUDZIWA. Kulibenso zokaikitsa zochuruka zina zilizonse. Mu M’kamphindi, m’kuthwanima kwa diso kudzakhala kuti kwatha, ndipo tidzakhala kuti tili kumbali inayo ndi okondedwa athu onse ndi IYE pa Mgonero wathu wa Ukwati.

NDIPO ICHO NDI CHIYAMBI CHABE …NDIPO KULIBE MAPETO!!

Bwerani mudzakonzekere Mgonero wa Chikwati uwu nafe Lamlungu lino pa 12:00 P.M., nthawi ya ku Jeffersonville, pamene Mulungu akuyankhula kupyolera mwa mngelo Wake wamphamvu, yemwe Iye anamutuma kuti adzatsogolere Mkwatibwi Wake, monga iye akuuzira, ndi kuwulula, zinsinsi zonse za Mulungu.

M’bale. Joseph Branham

Uthenga: 61-0806 – Sabata La Makumi Asanu Ndi Awiri La Daniele

25-0209 Cholinga Chofutukuka Pasanu Ndi Kamodzi Cha Gabrieli Kudzacheza Kwa Daniele

Uthenga: 61-0730E Cholinga Chofutukuka Pasanu Ndi Kamodzi Cha Gabrieli Kudzacheza Kwa Daniele

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mkwatibwi Wa kukondwera,

Tayang’ana nkhope zathu Kumwamba m’mapemphero ndi mapembedzero kuti tipeze tsiku ndi ola lomwe tikukhalamo.

Monga sizinachitikepo kale lonse, ife tikukhala pamodzi mu malo amwambamwamba, kuchokera kuzungulira dziko, kumva Mulungu akulankhula ndi kuwulula Mawu Ake kwa ife kupyolera mwa mngelo Wake wamphamvu wamthenga. Mngelo wapadziko lapansi wamthenga yemwe Atate anamutumiza kwa Mkwatibwi Wake mu tsiku lotsiriza ili kuti awulule Mawu Ake.

Gabrieli ndi mngelo wa anthu osankhidwa a Mulungu, Ayuda. Koma kwa Mkwatibwi Wake wa Amitundu, Melkizedeki Iyemwini anabwera ndipo anayankhula kupyolera mu thupi la munthu mwa mngelo wapadziko lapansi wotchedwa William Marrion Branham, kotero kuti Iye akhoze kulankhula ndi kuwulula Mawu Ake ONSE kwa Mkwatibwi Wake wokondedwa wapamtima.

Iye anali nalo ilo likujambulidwa, kusungidwa, ndi kusamaliridwa, kotero kuti Mkwatibwi akakhale ndi Chakudya Chake chauzimu, Manna obisika, mmanja mwawo miniti iliyonse ya tsiku lirilonse mpaka mapeto a nthawi.

Mkati mwathu ndimodzazidwa ndi kudzoza komweko pomwe tikunva Liwu la Mulungu kuwulula Mawu Ake kwa ife. Momwe Iye amavumbulutsira Mawu Ake kuti tithe kuwona bwino bwino ndi kumvetsetsa tanthauzo lake. Ilo likuwulula ola lomwe tikukhalamo, Limatiuza ife amene tiri ndi chimene chiti chichitike posachedwapa; Mkwatulo wathu ukubwera posachedwa.

Iye akuwululira kwa Mkwatibwi Wake zomwe ziti zichitike pano pa dziko lapansi pamene ife tiri naye Iye pa Mgonero wa Chikwati. Momwe Iye adzatsegula maso akhungu a osankhika ake; iwo amene Iye anawachititsa khungu chifukwa cha Mkwatibwi Wake wa Amitundu.

Abwenzi anga, ndikudziwa mmene tatopela ndi dziko lino ndipo tikulakalaka za kudza kwake kudzatichotsa, koma tiyeni tisangalale ndi kuyamikira zimene zikuchitika pakali pano pamaso pathu.

Tiyeni tikweze manja athu mmwamba, mitima yathu, mawu athu, ndi kukondwera. Osati kokha kuti tikuyembekezera zimene Iye ati atichitire posachedwapa, koma tiyeni tikondwere ndi zimene Iye akutiululira ndi kutichitira ife TSOPANO.

Iye akutiuza ife kuti ndife Mkwatibwi Wake wokonzedweratu akulumikizana limodzi ndi Iye ndi Mawu Ake. Iye akutitsimikizira mobwereza bwereza, ife tiri mu Chifuniro Chake changwiro pokhala ndi Liwu Lake, Mawu Ake, mngelo Wake. Iye Watipatsa ife CHIKHULUPIRIRO chodziwa ndi kuzindikira cha chomwe Ife tiri:
MAWU AKE OKHALA MTHUPI.

Tilibe kanthu koti tizikawopa; tilibe kanthu koti tizidandaula nako; tilibe kanthu koti kazitikwiyitsa. Kodi ndikudziwa bwanji zimenezo? MULUNGU ANANENA CHOMWECHO! CHONCHO TIYENI TIKONDWERE, KHALANI OSANGALALA, KHALANI OYAMIKILA; MAWU AMOYO AMAKHAKHALA NDI KUKHALA PAKATI PATHU. NDIFE MBEWU YAKE YAPAMWAMBA YAUFUMU.

Ine Zoonadi Ndikukhulupirira kuti Ambuye akuyeneranso kukhala wokondwa kudziwa kuti nthawi yafika ndipo tadzikonzekeretsa tokha pokhala wowona ndi mokhulupirika ku Mawu Ake.

Monga mnyamata wamng’ono yemwe anayang’ana pa kalilole kwa nthawi yake yoyamba, ife tikuyang’ana mu Mawu Ake, kuwona yemwe ife TILI. Ambuye…NDI INE. Ine ndine Mkwatibwi wa Mawu Anu amoyo. Ine Ndine amene munasankha. Ine ndiri mwa Inu, Inu muli mwa ine, ndife amodzi.

Kodi Ife sutingakondwerere bwanji ndi kukhala anthu osangalala kwambiri amene anakhalapo padziko lapansi? Oyera ndi aneneri onse tisanakhalepo ife ankafuna kukhala mu tsiku lino ndi kuwona malonjezo awa akukwanilitsidwa. Koma mwa CHISOMO cha Mulungu, Iye anatiika IFE kuno.

Sitingadikire:

Uuu, mai! [M’bale Branham akuwombetsa manja ake—Mkonzi.] Psyuu! Mwa kuyankhula kwina, pamene mdani akhala atachotsedwa, mapeto a tchimo abwera, kubweretsamo kwa chilungamo chosatha kutabwera, Satana akusindikizidwira mu dzenje lopandamalire, ndipo chidziwitso cha Ambuye chidzaphimba dziko lapansi monga madzi aphimbira nyanja. Ameni! Ulemerero kwa Mulungu! Izo zikubwera, m’bale, izo zikubwera!

Kodi ndi Kudzoza kotani kumene kudzakhala kukuchitika Lamlungu pa 12:00 P.M., nthawi yaku Jeffersonville, pamene ife tidzasonkhana palimodzi kuchokera kuzungulira dziko kuti tidzamve mngelo wa Mulungu, Liwu la Mulungu kwa Mkwatibwi, kutibweretsera ife Uthenga: Cholinga Chofutukuka Pasanu ndi Kamodzi Cha Gabrieli Kudzacheza Kwa Daniele 61-0730E.

M’bale. Joseph Branham

25-0202 Malangizo A Gabrieli Kwa Daniele

Uthenga: 61-0730M Malangizo A Gabrieli Kwa Daniele

PDF

BranhamTabernacle.org

Okondedwa Iwo Osankhidwa,

Ndi nthawi ya dzinja yabwino bwanji yomwe takhala tili nayo tikamaphunzira mibadwo isanu ndi iwiri ya mipingo, kenako Mulungu akuululanso zochuluka kwa ife mu Bukhu la Chibvumbulutso cha Yesu Khristu. Momwe machaputala atatu oyamba a Chibvumbulutso anali mibadwo ya mpingo, kenako momwe Yohane adatengedwera kunka ku mwamba mmutu wa 4 ndi 5 ndikutisonyeza zinthu zomwe zinali mkudza.

Mu mutu wa 6., Iye anaulula momwe Yohane adatsikira dziko lapansi kuti aone zinthu zomwe zikuchitika kuchokera ku mutu wa 6. Kuyambira mutu 19 wa buku la Chivumbulutso.

Mkwatibwi adzakhala wodalitsika bwanji Lamlungu pamene tikumva Liwu la Mulungu likulankhula kudzera mwa mngelo wake Wamphamvu wachisanu ndi chiwiri akutiuza ife chomwe chiti chiwululidwe patsogolo.

Ndine wokondwa kwambiri kunena kuti tsopano tiyamba kuphunzira kwakukulu masabata makumi asanu ndi awiri a Daniel. Mneneri ananena kuti icho chimangilira uthenga wonse tisanapite mu Zisindikizo Zisanu ndi ziwiri; Malipenga 7; Matsoka atatu; mkazi wovala dzuwa; kutulutsa a m’dierekezi wofiira; handiredi ndi forte-foro sauzande atasindikizidwa apo ; Zonse zikuchitika pakati pa nthawi ino.

Buku la Danieli ndi ndendende kalendala ya m’badwo ndi nthawi yomwe tikukhalamo ino, ndipo chingawoneke chovuta bwanji, Mulungu adzachiswa icho ndikuchipanga icho kukhala chophweka kwa ife.

Ndipo Mulungu akudziwa kuti ndizomwe ndikufuna tsopano, kuti nditonthoze anthu ake ndikuwauza chomwe chili pafupi, Onse a iwo m’mawa uno ndipo kudutsa ku mayiko omwe matepi awa adzapita, Pa dziko lonse lapansi, kuti tili kumapeto a nthawi.

Ndife anthu osankhidwa a Mulungu omwe akukhumba ndi kupempherera tsikulo ndi Ola limenelo. Ndipo maso athu akuyang’anila kumwamba, ndipo tikuyembekezera Iye kudza Kwake.

Tiyeni tonse tikhale ngati Danieli ndikuyang’ana nkhope zathu kumwamba, popemphera ndi mapembedzero, monga tikudziwa pa kuwerenga mawu ndi kumva Liwu lake, Kubwera kwa Ambuye kukuyandikira msanga; Tili kumapeto.

Tithandizeni Atate kuika cholemera chilichonse kumbali, tchimo lililonse, kusakhulupirira kwakung’ono kulikonse komwe kungatibwezere ife mmbuyo. Tsopano tiyeni tikambirane za mayitanidwe apamwamba, podziwa kuti nthawi yathu ndi yochepa.

Uthengawu Wapita kulinkonse. Chilichonse chakonzeka tsopano; Tikuyembekezera ndi kupuma. Mpingo wasindikizidwa. Oipa akuchita zoipa kwambiri. Mipingo ikukhala mpingo wokhuthala, koma oyera anu akubwera pafupi ndi inu.

Tili ndi Liwu likufuula m’chipululu, likuitana anthu kubwerera ku uthenga wa pachiyambi; Kubwerera ku zinthu za Mulungu. Timamvetsetsa mwa vumbulutso izi zinthu zomwe zikuchitika.

Bwerani mudzalumikizane nafe Lamlungu lino nthawi ya 12:00PM nthawi ya ku Jeffersonville , pomwe Mulungu akuwululira Mawu Ake kwa ife, pamene tikuyamba kuphunzira kwakukulu za buku la Danieli.

M’bale. Joseph Branham

61-0730M – Malangizo a Gabriel kwa Daniel

25-0126 Chibvumbulutso, Mutu Faivi Gawo II

BranhamTabernacle.org

Okondedwa Iwo Akupumula,

Ili ndilo Dzinja labwino kwambiri m’miyoyo yathu. Kudza kwa Ambuye kuli pafupi kumene. Ife tasindikizidwa ndi Mzimu Woyera; Chisindikizo cha Mulungu cha chivomerezo chakuti zonse zimene Kristu anafera ndi zathu.

Ife tsopano tiri ndi chikole cha cholowa chathu, Mzimu Woyera. Icho ndi Ndichitsimikizo, malipiro ochepera, kuti talandiridwa mwa Khristu. Ife tikupumula mu malonjezo a Mulungu, tikugona mu kutentha kwa Dzuwa Lake lowala; Mawu Ake otsimikiziridwa, kumvetsera ku Liwu Lake.

Ndicho chikole cha chipulumutso chathu. Ife Sitikudandaula ngati tipita Kumeneko kapena ayi, IFE TIKUPITA! Kodi tikudziwa bwanji zimenezi? Mulungu ananena chomwecho! Mulungu analonjeza ndipo ife tiri nacho chikole. Ife talandira kale Icho ndipo Khristu watilandira ife.

Palibe njira yothawira kwa Izo…m’malo mwake, tiri kumeneko! Zomwe tiyenera kuchita ndikungodikira; Iye ali pansi akuchita Chiwombolo Chachibale pakali pano. Ife tiri nacho chikole chake pakali pano. Ife tikungoyembekezera nthawi imene Iye abwereso Kwa Ife. Kenako, m’kamphindi, m’kuthwanima kwa diso tonse tidzapita ku Phwando la Ukwati.

Kungoganizira zonse zimene zili pa tsogolo pa ife. Malingaliro athu sangatengere zonse mkati. Tsiku ndi tsiku Iye akuwulula zambiri za Mawu Ake, kutsimikizira kuti malonjezo aakulu awa ndi athu.

Dziko likugwa; moto, zivomezi, ndi chipwirikiti kulikonse, koma amakhulupirira kuti ali ndi mpulumutsi watsopano amene adzapulumutsa dziko lapansi, ndikubweretsa m’badwo wawo wagolide. Talandira kale Mpulumutsi wathu ndipo takhala tikukhala mu nyengo yathu ya M’badwo wa Golide.

Tsopano Iye akutikonzekeretsa ife ku Chibvumbulutso chochuluka pamene ife tikulowa mu mutu wa Fayifi wa Chivumbulutso. Iye akukhazikitsa chochitika apa cha kutsegula kwa Zisindikizo Zisanu ndi ziwiri. Monga momwe iye anachitira mu mutu 1 wa Chivumbulutso, kutsegula njira ya Mibadwo Isanu ndi iwiri ya Mpingo.

Kodi zina zonse za Dzinja zidzakhala bwanji kwa Mkwatibwi? Tiyeni tiwone mwachidule:

Tsopano, ndilibe nthawi. Ine Ndazilemba izo pano. nkhani ina pa izo apa, koma msonkhano wathu wotsatira ife tisanalowe mu izi mwinamwake pamene ine ndidzachoka kutchuthi changa kapena nthawi ina, ine ndikufuna kuti nditenge masabata makumi asanu ndi awiri awa a Daniele ndi kumangiriza izo mkati momwe muno, ndi kuzisonyeza izo pamene izo zitengera izo ku chisangalalo cha Chipentekoste, ndi kuzibweretsa izo m’mbuyo kumene ndi miliri isanu ndi awiri iyo Zisindikizo Zisanu ndi ziwiri kuti zitsegulidwe pano ife tisanapite, ndi kusonyeza kuti izo ziri pa mapeto, izi…

Ndi nthawi yodabwitsa bwanji yomwe Ambuye wasungira Mkwatibwi Wake. Kudzivumbulutsa Yekha mu Mawu Ake kwa ife kuposa kale. Kutilimbikitsa kuti ndife osankhidwa ake amene Iye akuwadzera. Kutiuza ife kuti tiri mu chifuniro Chake Changwiro pakukhala ndi Liwu Lake, ndi Mawu Ake.

Kodi tikuchita chiyani? Osati chinthu chimodzi, Kungopumula! Kudikirira! Palibenso ntchito zolemetsa, palibenso zokhumudwitsa, TIKUPUMULA PA IZO!

Bwerani mudzapumule nafe Lamlungu lino pa 12:00 p.m., nthawi ya mu Jeffersonville, pamene ife tikumva Liwu la Mulungu LOTSIMIKIZILIDWA likutibweretsera ife Uthenga:
61-0618 – “Chivumbulutso, Mutu Fayifi Gawo II”.

M’bale. Joseph Branham

25-0112 Chibvumbulutso, Mutu Foro Gawo III

Uthenga: 61-0108 Chibvumbulutso, Mutu Foro Gawo III

PDF

BranhamTabernacle.org

Okondedwa Akumuyaya,

Ndi nthawi yoti tivule chovala chathu chankhondo ndi kuvala kuganiza kwanu kwa uzimu, chifukwa Mulungu akukonzekera kuti amupatse Mkwatibwi Wake Vumbulutso lochuluka la Mawu Ake.

Iye adzakhala akuvumbulutsa kwa ife zinsinsi zonse zakale. Iye adzatiuza zimene zidzachitike m’tsogolo. Zomwe ena onse m’Baibulo adangowona kapena kumva, Iye adzawulula tsatanetsatane wa chilichonse chaching’ono cha Mawu Ake ndi tanthauzo lake kwa ife.

Tidzamva ndi kumvetsa tanthauzo la zizindikiro za m’Baibulo: Zolengedwa Zamoyo, Nyanja Yagalasi, Mkango, Mwana wa Ng’ombe, Munthu, Mphungu, Mpando Wachifundo, Alonda, Akuluakulu, Ma liwu, Chirombo Chakuthengo Chosawetedwa, Zorengedwa za Moyo.

Tidzamva ndikumvetsetsa zonse za alonda a Chipangano Chakale. Yuda: Mlonda wa Kum’maŵa; Efraimu: Mlonda Wa Kumadzulo; Rueben: Mlonda waku Mmwela; ndi Dani: Mlonda wa Kumpoto.

Palibe chimene chikanakhoza kubwera paliponse mozungulira mpando wachifundo umenewo popanda kuwoloka mafuko amenewo. Mkango, luntha la munthu; Ng’ombe: kavalo wantchito; Mphungu: Kuthamanga kwake.

Momwe Kumwamba, dziko lapansi, pakati, ndi pozungulira, iwo anali alonda. Ndipo pamwamba pake panali Lawi la Moto. Palibe chinakhudza mpando wachifundo uwo popanda kudutsa mafuko amenewo.

Tsopano pali alonda a Chipangano Chatsopano: Mateyu, Marko, Luka ndi Yohane, kupita molunjika patsogolo. Chipata chakum’maŵa chimayang’aniridwa ndi mkango, chipata chakumpoto chimayang’aniridwa ndi chiwombankhanga chowuluka, Yohane, m’vangeri. Ndiye sing’anga wa mbali iyi, Luka, munthuyo.

Mauthenga anai a Uthenga Wabwino amateteza Madalitso a Chipentekoste ndi Lemba lirilonse kukhalira khonde ndendende zomwe iwo ananena. Ndipo tsopano Machitidwe a atumwi akuwonetsera lero ndi Mauthenga anai kuti Yesu Khristu ali yemweyo dzulo, lero, ndi nthawizonse.

Pamene wodzozedwa woona wa Mulungu ayankhula, Ilo ndi Liwu la Mulungu! Ife tikungofuna kufuula, “Woyera, woyera, woyera, kwa Ambuye!”

Palibe basi njira yopitira kutali kwa Icho. Ndipotu, ife sitingathe kuchoka kwa Icho, chifukwa Icho sichingatichokere kwa ife. Ndife odindidwa chisindikizo mpaka tsiku la chiombolo chathu. Palibe mtsogolo, palibe kalikonse, zowopsa, njala, ludzu, imfa, kapena CHINTHU, chimene chingatilekanitse ife ku chikondi cha Mulungu chimene chiri mwa Khristu Yesu.

Asanaikidwe maziko a dziko maina athu anayikidwa pa Bukhu la Moyo wa Mwanawankhosa kuti tiwone Kuwala UKU, kulandira Liwu Ili, kukhulupirira Uthenga Uwu, kulandira Mzimu Woyera wa tsiku lathu ndi kuyenda mwa Iwo. Pamene Mwanawankhosa anaphedwa, MAYINA ATHU anayikidwa pa Bukhu pa nthawi yomweyo Dzina la Mwanawankhosa linayikidwa pamenepo. ULEMERERO!!

Kotero, palibe chimene chingatilekanitse ife ku Uthenga uwu. Palibe chimene chingatilekanitse ife ku Liwu limenelo. Palibe chimene chingatenge Vumbulutso la Mawu Awa kwa ife. Ndi zathu. Mulungu anatiyitana ife ndipo anatisankha ife ndipo anatikonzeratu ife. Zonse ndi za Ife, Ndi zathu.

Pali njira imodzi yokha yopezera zonsezi. Inu Mukuyenera kutsukidwa ndi madzi a Mau. Inu mukuyenera kumva Mawu inu musanalowe mmenemo. Ndipo pali njira imodzi yokha imene inu mungafikire kwa Mulungu, ndiyo mwa Chikhulupiriro. Ndipo Chikhulupiriro chimadza pakumva, kumva Mawu a Mulungu, amene akunyezimiritsidwa kuchokera ku Malo Opatulikitsa kupita kwa mthenga wa m’badwowo.

Kotero, apa, mngelo wa m’badwo wa mpingo akunyezimira m’madzi awo Yemwe Munthu uyu ali muno, akunyezimiritsa chifundo Chake, Mawu Ake, chiweruzo Chake, Dzina Lake. Zonse zikuwonetseredwa muno pamene inu mumalekanitsidwa ndi kuzikhulupirira Izo. Kodi mukumvetsa?

Musati musiye kumvetsera kwa matepi, ingokhalani nawo Iwo. Fufuzani Izo ndi Mawu ndi kuwona ngati Izo ziri zolondola. Ndiyo Njira yoperekedwa ndi Mulungu ya lero.

Bwerani mudzakhale nafe Dzinja ili pamene tikulumikizana pamodzi kuchokera ku dziko lonse lapansi ndikumva Liwu la Mulungu likuwululira Mawu Ake kwa Mkwatibwi Wake kuposa kale. Palibe kudzoza kwakukulu kuposa kukanikiza kusewera ndi kumvetsera ku Liwu Lake.

Kuchokera pansi pamtima, nditha kunena kuti: Ndine wokondwa kunena kuti ndine Mmodzi wa Iwo ndi aliyense wa inu.

M’bale. Joseph Branham

Uthenga: 61-0108 – “Chivumbulutso, Mutu Foro Gawo III”
Nthawi: 12:00 PM. Jeffersonville nthawi