Category Archives: Uncategorized

25-0810 Zochitika Zamakono Zimamveka Bwino Ndi Uneneri

Uthenga: 65-1206 Zochitika Zamakono Zimamveka Bwino Ndi Uneneri

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mkwatibwi Woona ndi Wamoyo,

Pamene Yesu, Mawu Iwoeni, anabwera ku dziko lapansi zaka 2000 zapitazo, Iye anabwera monga Iye ananenera kuti Iye akanadzabwera, monga Mneneri. Mawu Ake amalengeza, kuti Iye asanabwere kachiwiri, mawonetseredwe athunthu a Umunthu wa Yesu Khristu adzawonetseredwa kachiwiri mu thupi, mwa mneneri. Mneneri ameneyo wabwera, dzina lake ndi William Marrion Branham.

Kodi wina aliyense angalephere bwanji kuzindikira kuti kumvera Liwu la Mulungu kumalankhula ndi iwo mwachindunji pa matepi kuti ndicho Chifuniro changwiro cha Mulungu? Ife tikudziwa kuti Mawu nthawizonse amadza kwa mneneri Wake; Sizingabwere mwanjira ina iliyonse. Izo ziyenera kubwera kupyolera mu njira ya Mulungu imene Iye anatiwuziratu kale za iyo . Ndi njira yokhayo yomwe Izo zidzadzere konse. Mulungu amayenda mu njira imene Iye analonjeza kuti Iye akanadzachita izo. Iye samalephera konse kuchita izo mwanjira yomweyo yofanana momwe Iye nthawizonse ankachitira.

Wina aliyense wa iwo ankadya chinthu chomwecho, iwo onse ankavina mu Mzimu, iwo onse anali nacho chirichonse mofanana; koma pamene izo zinafika ku nthawi yolekanitsidwa, Mawu ndi omwe analekanitsa. Mmomwe izo zirili lero! Mawu ndi omwe amalekanitsa! Pamene ifika nthawi yake,

Ife tikuwona kuti nthawi ikuchitika tsopano, Mawu akulekanitsa. Mkwatibwi akuimbidwa mlandu wa kuyika zochuluka kwambiri pa mneneri pamene iwo amati, “Pali amuna ena oyitanidwa ndi Mulungu, odzazidwa ndi Mzimu Woyera kuti atsogolere Mkwatibwi lero.” Inu mukusowa zochuluka kuposa matepi okha.Mulungu wayika amuna lero kuti atsogolere mpingo

“Iwe ukuyesera kumaganiza kuti ndiwe mmodzi wekha bwinoko kuposa izo. Ndipo iye anati, “Chabwino, gulu lonseli ndi loyera. Iwe ukuyesera kumadzipanga wekha…” Ngati ife tikanati tinene izo lero, kayankhulidwe ka pa msewu, “Nsangalabwi yokha ya pa doko.”

Ndipo Mose ankadziwa kuti Mulungu anali atamutuma iye uko chifukwa cha izo.

Mulungu ali nawo amuna odzazidwa ndi Mzimu Woyera kuti azitsogolera Mkwatibwi Wake; kuwatsogolera iwo KU PAKUTI ATERO AMBUYE, MNENERI MTHENGA. Pakuti Uthenga ndi m’thenga ali wofanana. Imeneyo ndiyo njira ya Mulungu yosasintha yoperekedwa ya tsiku la lero, ndiponso nthawi zonse.

Chifukwa iwo anamvetsera kwa cholakwika. Pamene Mose, wotsimikizidwira ndi Mulungu, ndi mtsogoleri kuti awasonyeze iwo njira yaku Dziko Lolonjezedwa, ndipo iwo anali atabwera patali chotere bwinobwino, komano iwo sakanakhoza kupitirira limodzi naye.
Tsopano, okhulupirira akhoza kuwaona Iwo, koma osakhulupirira sangakhoze kuwawona Iwo akutsimikizidwira.

Osati kokha kuti inu munasankhidwa kuti mulandire Vumbulutso lalikulu la nthawi yotsiriza ili la lero, koma Mulungu, mwa njira ya matepi Ake a Chakudya chosungidwa, amalankhula pakati pa mizere kwa Mkwatibwi Wake wokoma wa pamtima.

Ndiye ngati inu muli mwana wamwamuna wa Mulungu kapena mwana wamkazi wa Mulungu, inu munali mwa Mulungu nthawiyonseyo. Koma Iye ankadziwa kama wake ndi nthawi yomwe inu mukanati mudzabzalidwe. Kotero tsopano inu mwapangidwa cholengedwa, mwana wamwamuna wa Mulungu, mwana wamwamuna kapena wamkazi wa Mulungu wowonetseredwa kuti mukomane ndi chitsutso cha ora lino kuti mutsimikizitsire Mulungu woona ndi wamoyo wa ora lino, Uthenga umene ukubwerapowu mu nthawi ino. Uko nkulondola! Inu munapangidwa uko asanakhazikitsidwe maziko a dziko.

Ndi kalata yachikondi bwanji yapakati pa mizere kwa Mkwatibwi Wake, ULEMERERO!!! Osati kokha kuti Iye anatidziwa ndi kutisankha ife asanaikidwe maziko a dziko, koma pano Iye akutiuza ife kuti Iye anatisankha ife kuti tikhale ana Ake aamuna ndi aakazi owonetseredwa a LERO. Iye anatiika ife pano pa dziko lapansi lero, pamwamba pa oyera mtima ena onse kuyambira pachiyambi, chifukwa Iye ankadziwa kuti ife tikanati tidzakumane ndi vuto la ora lino kuti titsimikizire Mulungu woona ndi wamoyo wa ora lino, Uthenga umene ukubwera mu nthawi ino.

Ife tinali mwa Mulungu, jini, mawu, chikhumbo kuchokera kuchiyambi, koma TSOPANO Ife tikukhala PAMODZI mu malo Ammwambamwamba mwa Khristu Yesu, kuyankhulana ndi Iye mwa Mawu Ake, kupyolera mu Mawu Ake; pakuti ife NDIFE MAWU AKE, ndipo Iwo akudyetsa miyoyo yathu.

Sitingathe, ndipo sitidzabayilamo kalikonse m’miyoyo yathu koma Mawu osaipitsidwa a Mulungu. Timazindikira ndikukhulupirira kuti ndi njira yoperekedwa ndi Mulungu ya lero.

Ife tikanakonda kuti inu mubwere kuzajowinana nafe Lamlungu lino pa 12:00 p.m., nthawi ya ku Jeffersonville, pamene ife tikumva LIWU LOKHA, Liwu la Mulungu pa matepi, inu mukhoza kunena kuti AMEN kwa Mawu aliwonse omwe inu mumawamva.

M’bale. Joseph Branham

Uthenga: Zochitika Zamakono Zimamveka Bwino Ndi Uneneri 65-1206

Malemba oti muwerenge musanamve Uthenga:

Genesis 22
Deuteronomo 18:15
Masalimo 16:10 / 22:1 / 22:18 / 22:7-8 / 35:11
Yesaya 7:14 / 9:6 / 35:7 / 50:6 / 53:9 / 53:12 / 40:3
Amosi 3:7
Zekariya 11:12; 13:7/14:7
Malaki 3:1/4:5-6
Mateyu woyera 4:4 / 24:24 / 11:1-19
Luka woyera 17:22-30 / 24:13–27
Ahebri 13:8; 1:1
Yohane Woyera 1:1
Chivumbulutso 3:14-21; 10:7

25-0803 Zinthu Zimene Ziti Zidzakakhaleko

Uthenga: 65-1205 Zinthu Zimene Ziti Zidzakakhaleko

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Zikhumbo za Mulungu,

Mawu aliwonse amene analankhulidwa mu Uthenga uwu ndi kalata yachikondi kwa Mkwatibwi Wake. Kuganiza kuti Atate wathu wa Kumwamba amatikonda kwambiri, moti sikuti ankangofuna kuti tiziwerenga Mawu ake, koma ankafuna kuti tizimva Liwu lake likulankhula ku mitima yathu kuti atiuze kuti: “Inu ndinu liwu langa lamoyo, Chikhumbo changa chamoyo, chimene Ine ndingawonetsere pa dziko lapansi.

Ndiyeno kuganiza kuti pambuyo pa nsembe Yake yonse imene Iye anachita pano pa dziko lapansi, moyo umene Iye anakhala, njira imene Iye anayenda. Iye anapempha chinthu chimodzi,

“Kuti kumene Ine ndikakhale, iwonso akakhaleko.” Iye anapempha chiyanjano chathu. Ndicho chinthu chokhacho chimene Iye anawapempha Atate mu pemphero, ubwenzi wanu wosatha.

Kumene ine ndiri, “Mawu Ake,” ifeso tiyenera kukakhalako, kuti tikalandire chiyanjano Chake, Ubwezi Wake Wosatha, kwanthawizonse. Chotero, tiyenera kukhala moyo mwa Mawu aliwonse amene Iye analankhula kwa ife pa matepi kuti tikhale Namwali m’kwatibwi wa mawu, amene amatipanga ife gawo la Mkwati.

Ilo ndilo VUMBULUTSO la Yesu Khristu mu ora lino. Osati chimene Iye anali mu ora lina, yemwe Iye ali TSOPANO. Mawu a lero. Kumene Mulungu ali lero. Ndilo Vumbulutso la lero. Tsopano likukula mwa Mkwatibwi, kutipanga ife mu m’thunthu lokwana la mngwiro la ana aamuna ndi aakazi.

Ife timadziwona tokha mu Mawu Ake. Ife tikudziwa amene ife tili. Ife tikudziwa ife tiri mu dongosolo Lake. Iyi ndi Njira yoperekedwa ndi Mulungu ya lero. Ife tikudziwa Mkwatulo uli pafupi. Posachedwapa okondedwa athu adzawonekera. Kenako tidzadziwa: kuti Ife Tafika. Ife tonse tikupita Kumwamba…inde, Kumwamba, malo enieni monga awa.

Ife tikupita kumalo enieni kumene tizikachitako zinthu, kumene tikakhalako moyo. Ife tizikagwirako ntchito. Ife tikasangalalako. Ife tikakhalako moyo. Ife tikupita ku Moyo, ku Moyo Wamuyaya weniweni. Ife tikupita Kumwamba, paradiso. Chimodzimodzi monga momwe Adamu ndi Eva ankagwirira ntchito, ndi kumakhala moyo, ndi kumadya, ndi kumasangalalako, mmunda wa Edeni tchimo lisanabweremo, ife tiri panjira yathu tikubwerera kumeneko panonso, kulondola, tikubwerera kumeneko. Adamu woyamba, chifukwa cha tchimo, anatichotsako ife. Adamu Wachiwiri, kupyolera mu chirungamo, akutibwezeretsako ife kumeneko kachiwiri; akutilungamitsa ife ndi kutibwezeretsanso ife mmenemo.

Kodi aliyense anganene bwanji za izi pazomwe izo zikutanthauza kwa ife? Chowonadi ndi chakuti tikupita ku paradaiso kumene tikukakhala kwa Muyaya wonse pamodzi. Kulibenso chisoni, zowawa kapena Zokhumudwitsa, ungwiro basi pa ungwiro.

Mitima yathu ikukondwera, miyoyo yathu ili pamoto mkati mwathu. Satana akumayika mochuruka ndi mochuruka zopsinja pa ife tsiku lililonse , koma ife tikusangalalabe. Chifukwa:

  • TIKUDZIWA, YEMWE IFE TILI.
  • TIKUDZIWA, SITINAMULEPHERE, NDIPO SITIDZAMULEPHERA IYE.
  • TIKUDZIWA, TILI MU CHIFUNIRO CHAKE CHANGWIRO.
  • TIKUDZIWA, WATIPATSA IFE VUMBULUTSO LOWONA LA MAWU AKE.

M’bale Joseph, inu mumalemba chinthu chomwecho sabata iliyonse. ULEMERERO, ndidzalemba chimenecho sabata iliyonse chifukwa Iye akufuna kuti inu mudziwe mochuruka momwe Iye amakukonderani inu.Yemwe inu muli. Kumene inu mukupita. Chithunzi chikusandulika kukhala chenicheni. Inu ndinu Mawu mukusandulika kukhala Mawu.

Okondedwa dziko, bwerani mudzajowinane nafe Lamlungu lino pa 12:00 p.m., nthawi ya ku Jeffersonville, polumikizana, osati chifukwa “Ine” ndikukuitanani inu, koma chifukwa “IYE” akukuitanani inu. Osati chifukwa “Ine” ndinatenga tepiyo, koma kumva Mawu ndi gawo la Mkwatibwi kuzungulira dziko lonse nthawi imodzi.

Kodi Ife tingazindikire kuti n’zotheka kuti Mkwatibwi amve Liwu la Mulungu padziko lonse, pa nthawi yofanana? Ameneyo ayenera kukhala Mulungu. Mulungu anali ndi mneneri wake kuti achite izo pamene mngelo Wake anali pano pa dziko lapansi. Iye analimbikitsa Mkwatibwi kulumikizana mu m’pemphero, ONSE PA NTHAWI YOFANANA YA KU JEFFERSONVILLE, 9:00, 12;00, 3:00; Kodi icho ndi chinthu chachikulu motani tsopano, kuti Mkwatibwi akhoza kulumikizana ngati M’MODZI kuti amve Liwu la Mulungu likuyankhula kwa iwo onse pa nthawi imodzi?

M’bale. Joseph Branham

Uthenga: Zinthu Zimene Ziti Zidzakakhaleko 65-1205

Malemba:
Mateyu woyera 22:1-14
Yohane Woyera 14:1-7
Ahebri 7:1-10

25-0727 Mkwatulo

Uthenga: 65-1204 Mkwatulo

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mkwatibwi Wopanda mangawa,
 
 
Ambuye anatipatsa ife nthawi yodabwitsa kwambiri pa msasa sabata yatha pamene Iye anatiululira Mau ake kwa ife. Iye anatsimikizira, mwa Mawu Ake, kuti Mtheradi wathu uli: Mawu Ake, Uthenga uwu, Liwu la Mulungu pa matepi; onse ali ofanana, Yesu Kristu yemweyo dzulo, lero, ndi kunthawi zonse. 
 
Tinamva mmene mdierekezi amayesera kulekanitsa Uthenga kwa mthengayo, koma Ambuye Yesu alemekezeke, Mulungu mwini analankhula kudzera mwa mngelo wake wamphamvu natiuza kuti:

Ife tikupeza apo kuti pamene munthu abwera, atatumidwa kuchokera kwa Mulungu, wodzozedwa ndi Mulungu, ndi PAKUTI ATERO AMBUYE woona, uthenga ndi mtumiki ali mmodzi ndi ofanana. Chifukwa iye watumidwa kuti adzayimire PAKUTI ATERO AMBUYE, Mawu ndi Mawu, kotero iye ndi uthenga wake ali ofanana.

Inu simungakhoze kulekanitsa Uthenga kwa mtumikiyo, iwo ali ofanana, PAKUTI ATERO AMBUYE. Ziribe kanthu zomwe wodzozedwa wabodza aliyense akunena, Mulungu anati iwo ali ofanana ndipo sangalekanitsidwe.
 
Ndiye Iye anatiuza ife kuti sitikusowa chiguduli chosefera kuti tigwire zipumbu zonse pomwe ife tikumvetsera ku matepi, pakuti mulibe nsikidzi kapena madzi a sikidzi mu Uthenga uwu. Ndi chitsime Chake cha kasupe chomwe chimayenda madzi nthawi zonse oyera ndi awukhondo. Nthawizonse akutumphukabe pamwamba, sichimawuma ayi, kumangopitirira kukankhira ndi kukankha, kumatipatsa ife Vumbulutso lochulukira la Mawu Ake.
 
Anatikumbutsa kuti tisaiwale kuti pangano lake ndi ife ndi Losatsutsika, Losatsutsika, koma koposa zonse, Lopanda mangawa.
 
Kaya ndi chikondi, chithandizo, kapena kugonja, ngati china chake chopanda mangawa ndi MTHERADI ndipo sichigwirizana ndi mfundo kapena zikhalidwe zina zapadera: izo zichitika zivute zitani.
 
 Ndiye Iye anafuna kukhomerera msomali, kotero anatiuza ife kuti lero Malemba Ake akukwaniritsidwa pamaso pathu.

Kuti d-z-u-w-a lomwelo limene limatuluka kummawa ndi d-z-u-w-a lomwelo limene limadzalowa kumadzulo. Ndipo M-w-a-n-a wa Mulungu yemweyo amene anabwera kummawa ndi kudzadzitsimikizira Yekha ngati Mulungu wowonetseredwa mu thupi, ndi M-w-a-n-a wa Mulungu yemweyo kumadzulo kwa dziko lapansi kuno, amene akudzizindikiritsa Yekha pakati pa mpingo usikuuno, yemweyo dzulo, lero, ndi kwanthawizonse. Kuwala kwa kumadzulo kwa Mwana kwafika. Lero Lemba ili lakwaniritsidwa pamaso pathu.

 Mwana wa Munthu wabweranso mu thupi laumunthu mu tsiku lathu, monga momwe Iye analonjezera kuti Iye akanadzatero, kuti adzaitane Mkwatibwi. Ndi Yesu Khristu akuyankhula molunjika kwa ife, ndipo Izo sizikusowa kutanthauzira kwa munthu. Zonse zomwe tikusowa, zomwe tikufuna, ndi Liwu la Mulungu loyankhula pa tepi lochokera kwa Mulungu Mwiniwake.

Ndi vumbulutso la kukwaniritsika kwa Mawu kukhalitsidwa owona. Ndipo ife tikukhala mu tsiku limenelo. Mulungu alemekezeke! Vumbulutso la chinsinsi la Iyemwini.

Ndi nthawi yaulemerero bwanji yomwe Mkwatibwi ali nayo, ali mu kukhalapo kwa Mwana, akucha. Tirigu wabwereranso ku tirigu, ndipo palibe chotupitsa pakati pathu. Liwu loyera la Mulungu loyankhula kwa ife, kutiumba ndi kutipanga ife mu chifaniziro cha Khristu, Mawu.
 
 
Ife ndife ana aamuna ndi aakazi a Mulungu, chikhumbo Chake chimene Iye anachikonzeratu kuti chibwere mu m’badwo uno, m’badwo waukulu kwambiri mu mbiriyakale ya dziko.  Iye ankadziwa kuti ife sitikanati tilephere, ife sitikanati tinyengerere, koma ife tikanakhala Mkwatibwi Wake wa Mawu owona ndi wokhulupirika, Mbewu Yake Yachifumu yolonjezedwa Yapamwamba ya Abrahamu yomwe inali nkudza.
 
Mkwatulo uli pafupi. Nthawi yafika kumapeto. Iye akudzera Mkwatibwi Wake yemwe wadzikonzekeretsa Yekha koma akukhala mu Kukhalapo kwa Mwana, akumva Liwu Lake kumuveka Mkwatibwi Wake. Posachedwapa tidzayamba kuona okondedwa athu omwe ali kuseri kwa ketani ya nthawi, omwe akuyembekezera ndi kulakalaka kukhala nafe.

Matepi ndi njira yoperekedwa ndi Mulungu kuti afikitse Mkwatibwi Wake ku ungwiro. Matepi awa ali chinthu chokha chimene chidzagwirizanitsa Mkwatibwi Wake. Matepi awa ali Liwu la Mulungu kwa Mkwatibwi Wake.
 
Ine ndikukuitanani inu kuti mubwere ndi kudzalumikizana nafe, gawo la Mkwatibwi Wake, Lamlungu lino pa 12:00 p.m., nthawi ya ku Jeffersonville, pamene ife tikumva zonse za zomwe zikukonzekera kuti zichitike posachedwapa: Mkwatulo 65-1204. 

 
M’bale. Joseph Branham

25-0720 Pa Mapiko A Nkhunda Yoyera-mwachipale

Uthenga: 65-1128E Pa Mapiko A Nkhunda Yoyera-mwachipale

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mkwatibwi wa Khristu, tiyeni ife tibwere palimodzi Lamlungu 12:00 P.M., nthawi ya ku Jeffersonville, kuti tidzamve 65-1128E Pa Mapiko A Nkhunda Yoyera-mwachipale
M’bale. Joseph Branham

25-0713 Malo Okhawo Operekedwa Ndi Mulungu Opembedzerapo

Uthenga: 65-1128M Malo Okhawo Operekedwa Ndi Mulungu Opembedzerapo

PDF

BranhamTabernacle.org

Lokondedwa Banja la Yesu Khristu,

Chinachake chikuchitika kuposa kale ndi Mkwatibwi wa Khristu padziko lonse lapansi. Zinthu zomwe tazimva ndi kulakalaka kuziwona tsopano zikuwonetseredwa pamaso pathu.

Mzimu Woyera ukugwirizanitsa Mkwatibwi Wake monga Iye anati Iye akanadzatero, mwa njira Yake YOKHA yoperekedwa ya lero, Liwu la Mulungu pa matepi.

Iye akuwulula ndi kutsimikizira Mawu Ake kuposa kale. Mofanana ndi chitsime cha kasupe, Chibvumbulutso chikutumphuka mkati mwathu.

Chilumikizano chauzimu chija cha Khristu ndi Mpingo Wake tsopano, pamene mnofu ukusandulika Mawu, ndipo Mawu akusandulika mnofu, kuwonetseredwa, kutsimikiziridwa. Basi zomwe Baibulo linati zikanadzachitika mu tsiku lino, izo zikuchitika, tsiku ndi tsiku. Bwanji, izo zikuwunjikana mofulumira kwambiri kunja uko, mu zipululu izo, ndi zinthu zomwe zikuchitika, mokuti ine sindingakhoze ngakhale kuyendera limodzi nazo izo.

Tsiku ndi tsiku Chivumbulutso chochuluka chikuwululidwa ndikuwonetseredwa kwa ife. Monga mneneri, zinthu zikuchitika ndipo zikuchitika mofulumira kwambiri, sitingathe ngakhale kupitiriza nazo … ULEMERERO!!!

Nthawi yathu yafika. Lemba likukwaniritsidwa. Thupi likukhala Mawu, ndipo Mawu akukhala thupi. Basi zomwe mneneri ananena kuti zikanadzachitika tsopano zikuchitika.

Kodi ndi Chifukwa chiyani ife?

Palibe chotupitsa, kapena mawu osadziwika, palibe kutanthauzira kwa munthu kofunika pakati pathu. Timangomvetsera Mawu Oyera Angwiro kuchokera mkamwa mwa Mulungu pamene Iye akulankhula kwa ife milomo ndi khutu.

Tsopano ife tikuwaona Mawu olonjezedwa omwewo, a Luka, a Malaki, malonjezo onse awa kuyambira lero, akupangidwa thupi, akukhala pakati pa ife, amene ife tinawamva ndi makutu athu; tsopano ife tikumuwona Iye (ndi maso athu) akutanthauzira Mawu Ake Omwe, ife sitikusowa kutanthauzira kulikonse kwa munthu.

Mkwatibwi, izo mophweka sizikanakhoza kumveka bwino kuposa izo. Iye ndi Mulungu, atayima pamaso pa Mkwatibwi Wake mu thupi laumunthu, yemwe ife tikhoza kumuwona ndi maso athu omwe, akuyankhula ndi kutanthauzira Mawu Ake Omwe, ndi kuwayika iwo pa tepi. Mawu Angwiro olankhulidwa ndi kulembedwa ndi Mulungu Mwiniwake, motero samasowa kutanthauzira kulikonse kwa munthu.

  • Mulungu akuyankhula molunjika kwa Mkwatibwi Wake, pa matepi.
  • Mulungu akutanthauzira Mawu Ake Omwe, pa matepi.
  • Mulungu akudziwulula Yekha, pa matepi.
  • Mulungu akumuuza Mkwatibwi Wake, inu simukusowa kutanthauzira kulikonse kwa munthu, Mawu Anga pa matepi ali zonse ZOFUNIKIRA MKWATIBWI WANGA.

Kumbukirani, pamene inu muchoka pano, muyambe kuchokamo mu mankhusu tsopano; inu mukupita mu njere, koma mukakhale mu Kukhalapo kwa Mwana. Musakawonjezere, zimene ine ndanena; musakachotsere, zimene ine ndanena. Chifukwa, ine ndimayankhula Choonadi monga momwe ine ndikudziwira Icho, monga Atate andipatsira ine. Mukuona?

Mulungu wapanga NJIRA YABWINO YOKHAYO kuti Mkwatibwi achite monga momwe anatilamulira ife. Izi sizinachitikepo, mpaka lero. Palibe kungoganiza, popanda kudabwa, palibe funso ngati pali china chowonjezera, chochotsedwa, kapena kutanthauzira. Mkwatibwi wapatsidwa Chibvumbulutso chenicheni: KUSEWERA MATEPI NDI NJIRA YABWINO YA MULUNGU.

Ngati zingachitike, ndiroleni ndinenenso. Vumbulutso langa liri kuti Mkwatibwi wa Yesu Khristu, osati ena, MKWATIBWI, sasowa CHINTHU CHINA CHILICHONSE AYI koma Liwu la Mulungu pa matepi.

Koma pamene Mzimu Woyera uwo kwenikweni Mawu enieni abwera mwa inu (Mawu, Yesu), ndiye, m’bale, Uthenga si chinsinsi kwa inu kenako; inu mukuchidziwa Icho, m’bale, Icho chonse chawala pamaso panu.

Uthenga si chinsinsi kwa ine. Yesu Khristu ali yemweyo dzulo, lero, ndi kunthawi zonse. Kumwamba ndi dziko lonse lapansi zimatchedwa Yesu. Yesu ndiye Mawu.

Ndipo Dzinalo liri mu Mawu chifukwa Iye ali Mawu. Ameni! Iye ndi chiyani ndiye? Mawu otanthauziridwa ndi mawonetseredwe a Dzina la Mulungu.

Mulungu akulumikiza Mkwatibwi Wake ndi Liwu Lake, limene Iye analilemba ndi kulisungira kwa lero, kotero kuti Iye akhoze kubweretsa Mkwatibwi Wake palimodzi ngati Chigawo Chimodzi. Mkwatibwi aziwona izo ndi kuzizindikira Iyo ngati NJIRA YOKHAYO yomwe Iye angakhoze kubweretsa Mkwatibwi Wake palimodzi.

Iye anachita zimenezi zaka zoposa 60 zapitazo kuti atisonyeze mmene angachitire zimenezi masiku ano. Ndife “m’modzi mwa mipingo yake yomwe ikugwirizana”

Ngati ine sindikhulupirira mu kupita kutchalitchi, nchifukwa chiyani ine ndiri ndi tchalitchi? Ife tinali nawo iwo onse kudutsa m’dzikoli, titalumikizitsana usiku wina, mailosi thuu handiredi aliwonse a mabwalo anali ndi imodzi ya matchalitchi anga.

Atumiki ambiri amauza mipingo yawo kukhala pa “kulumikizana” kapena “kukhamukira”, “kumvera Uthenga womwewo nthawi imodzi”, sikupita kutchalitchi. IYE ANANGOTI IZO ZINALI! Iwo mwina sakudziwa Mawu kapena sangathe kuwerenga kalata yachikondi monga Mkwatibwi angachitire.

Kodi mpingo ndi chiyani? Tiyeni tingowona zomwe M’bale Branham ananena kuti zinali mpingo.

Magulu ambirimbiri, ali nawo malo awa omwe inu nonse munali nawo kuno kuchokera ku kachisi. Izo zalumikizidwanso ku Phoenix, kuti kulikonse kuli msonkhano, izo zikufika kumene umo…Ndipo iwo akusonkhana mu matchalitchi ndi mmanyumba, ndi zinthu monga choncho, zikudutsa mu mpweya wa mawu wabwino kwambiri.

M’bale Branham akunena momveka bwino kuti anthu mu “nyumba” zawo ndi “zinthu zonga izo” inali imodzi mwa mipingo yake yomwe inali yolumikizana. Motero nyumba, malo opangira mafuta, nyumba, mabanja osonkhanitsidwa pamodzi pa hook up ake anapanga mpingo.

Tiyeni tiwerenge KALATA YA CHIKONDI mwakanthawi kochurukilapo pang’ono

Ife tikupempherera mipingo yonse ndi magulu amene asonkhana pozungulira zo—zo—zoyankhulira zazing’ono kunja kudutsa, kuchokera ku fukoli, njira yonse mpaka ku Gombe la Kumadzulo, kukwera mpaka ku mapiri a Arizona, kutsika mpaka ku zigwa za Texas, njira yonse mpaka ku Gombe la Kummawa, monse kudutsa dziko, Ambuye, kumene iwo asonkhana. Maora ambiri motalikana, ife tiri mu nthawi, koma, Ambuye, ife tiri limodzi usikuuno ngati chimango chimodzi, okhulupirira, tikuyembekezera Kudza kwa Mesiya.

Kotero kukhala pa Kulumikizana, kumvetsera kwa M’bale Branham ONSE PA NTHAWI YOFANANA; iwo anali pamodzi ngati gulu limodzi, okhulupirira, kuyembekezera Kudza kwa Mesiya.

Koma mukunena kuti ngati muchita izi lero, kuti uko sindiko kupita kutchalitchi, izo ndizolakwika, sikumasonkhana pamodzi monga momwe tikuwonera tsiku likuyandikira, sikupita kutchalitchi kodi?

Ndiroleni ine ndikufunseni inu funso ndipo inu muwayankhe osonkhana anu. Ngati M’bale Branham akanakhala pano lero, mu thupi, ndipo inu mukanakhoza kukhamukira kapena kulumikizana kuti mumumve iye Lamlungu lirilonse mmawa, Onse pa nthawi imodzi ndi Mkwatibwi kuzungulira dziko, azibusa, kodi inu mungagwirizane ndi kumumva M’bale Branham kapena kodi inu mungalalikire?

M’bale Branham momveka akunena kuti ntchito yanu ndi mpingo wanu. Ngati inu munali kuno zaka makumi asanu ndi chimodzi zapitazo ndipo M’bale Branham anali ndi utumiki, koma mpingo wanu sunapiteko koma kukhala ndi utumiki wawo (umene atumiki ambiri ankachitira kalelo), kodi inu mungapite ku “mpingo wanu”, kapena kodi inu mungapite ku “Branham Tabernacle” kuti mukamve M’bale Branham?

Ndikupatsani yankho langa. Ine ndikanakhala nditaima pakhomo mu mvula, matalala kapena mphepo yamkuntho kuti ndilowe mu Kachisi kuti ndimve mneneri wa Mulungu. Ngati ndikanapita ku mpingo wina uja, ndikanasintha matchalitchi usiku womwewo.

Koma mkazi ameneyo, iye sankadziwa ngati mphamvu inali mu ndodo kapena ayi, koma iye ankadziwa kuti Mulungu anali mwa Eliya. Ndiko kumene Mulungu anali: mwa mneneri Wake. Iye anati, “Monga Ambuye ali wa moyo, ndiye kuti solo yanuso ili moyo, ine sindidzakusiyani inu.”

Ine ndikukuitanani inu kuti mutijowine ife ndi kukhala mmodzi wa mipingo ya M’bale Branham pa nthawi yolumikizirana Lamlungu 12:00 P.M., nthawi ya ku Jeffersonville, pamene ife tikumva Liwu la Mulungu likutibweretsera ife Uthenga: Malo Okhawo Operekedwa Ndi Mulungu Opembedzerapo 65-1128M.

M’bale. Joseph Branham

25-0706 Ine Ndakhala Ndikumva Koma Tsopano Ine Ndawona

Uthenga: 65-1127E Ine Ndakhala Ndikumva Koma Tsopano Ine Ndawona

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mkwatibwi Wolumikizidwa,

Lero, Mawu awa amene Mulungu analankhula kupyolera mwa Mngelo Wake Wachisanu ndi chiwiri akukwaniritsidwabe kupyolera mwa IFE, MKWATIBWI WA YESU KHRISTU.

Ngati ine sindikhulupirira mu kupita kutchalitchi, nchifukwa chiyani ine ndiri ndi tchalitchi? Ife tinali nawo iwo onse kudutsa m’dzikoli, titalumikizitsana usiku wina, mailosi thuu handiredi aliwonse a mabwalo anali ndi imodzi ya matchalitchi anga.

Iwo anali m’matchalitchi, m’nyumba, m’nyumba zing’onozing’ono, ndipo ngakhale pokwerera mafuta; anamwazikana kudutsa United States, akumvetsera, zonse pa nthawi imodzi yomweyo pomwe Mawu anali kupita.

Ndipo lero, ife tikadali MMODZI WA MIPINGO YAKE. Iye akadali M’BUSA WATHU. Mawu Ake SAMASOWABE KUTANTHAUZIDWA, ndipo ife tikanali osonkhanitsidwa pa dziko lonse, WOl pa MODZI, kumvetsera ku LIWU la Mulungu kumupanga kukhala wa gwiro Mkwatibwi wa Yesu Khristu.

Lero, Mawu awa akukwaniritsidwabe.

N’cifukwa ciani anali kucita zimenezo kalelo? Chifukwa chiyani abusa anatseka mipingo yawo kuti asamvere Uthenga nthawi yomweyo? Iwo akanangoyembekezera kuti atenge matepi, ndiyeno nkumalalikira Uthenga iwoeni kwa anthu awo kenako; ndipo ndikutsimikiza kuti ambiri opanda bvumbulutso Ankachita izi.

Kapena mwinamwake ena adawuza mipingo yawo, “Tsopano mvetserani, ife timakhulupirira M’bale Branham kuti ndi mneneri wa Mulungu, koma iye sananene kuti ife timayenera kumamvetsera kwa iye mu mipingo yathu. Ine ndikulalikira Lamlungu lino, ndi Lamlungu lirilonse;

Kenako Mkwatibwi , monga Mkwatibwi chabe tsopano, anali ndi Vumbulutso, ndipo ankafuna kumva Liwu la Mulungu mwachinjunji kwa iwo eni. Iwo ankafuna kuti akhale olumikizana ndi Mkwatibwi kuzungulira dziko kuti amve Liwu la Mulungu pamene ilo linali kunveka. Iwo ankafuna kuti azindikiritsidwe ngati umodzi wa mipingo yake, nyumba, kapena kulikonse kumene iwo anali, ndi Uthenga, Liwu, ndipo tsopano matepi.

Lero, Mawu awa akukwaniritsidwabe.

Chifukwa chiyani iwo/ife tinachiwona Icho ndipo ena sanachiwone? Mwa kudziwiratu, ife tinadzozedweratu kuti tiziwone Izi. Koma inu amene simunadzozedwe, simudzaziwona konse Izo. Tirigu akuwawona Iwo ndipo wayamba kuchokapo.

Izi sizikutanthauza kuti muyenera kusiya kupita kutchalitchi chanu. Komanso sizikutanthauza kuti abusa anu asiye kutumikira. Mophweka izi Zikutanthauza kuti mautumiki ambiri ndi azibusa aiwala CHINTHU CHENICHENI, ndiko kusawawuza anthu awo kuti MAWU OFUNIKA KWAMBIRI omwe muyenera kuwamva ndi LIWU la Mulungu pa matepi.

Kupita ku tchalitchi tsiku lililonse sabata iliyonse sikukupanga iwe kukhala Mkwatibwi; chimenecho sichofunikira cha Mulungu. Afarisi ndi Asaduki anali ndi chiphunzitso chimenecho kumusi uko. Iwo ankadziwa chilembo chirichonse cha Mawu aliwonse, koma Mawu Amoyo anali ataima POMWEPO mu thupi la munthu, koma kodi iwo anachita chiyani? Chinthu chomwecho chimene ambiri amachita lerolino.

Iwo amati, “Izo zinali zipembedzo zimene iye anali kuzikamba.” Iwo samamulola M’bale Branham mu mipingo yawo kuti azilalikira, koma ife timalalikira Mawu ndi kunena mobwereza basi zomwe iye ananena.

Izi ndizodabwitsa. Ambuye alemekezeke. Ndi zomwe muyenera kuchita. Koma Kenako mkumati, lero ndi zosiyana, ndi zolakwika kumasewera matepi a M’bale Branham mu tchalitchi chanu. Inu apo simuli osiyana ndi Afarisi ndi Asaduki, kapena zipembedzo.

Ndiwe wa chinyengo.

Monga zinaliri pamenepo, Ndi Yesu, atayima pakhomo akugogoda, kuyesera kuti alowe kuti ayankhule mwachinjunji kwa Mpingo Wake, ndipo iwo sadzatsegula zitseko zawo, ndipo sadzasewera matepi mu mipingo yawo. “Iye sakubwera mu mpingo wathu ndi kudzalalikira”.

Mdaniyo azipotoza izo ndikuzivunguza mbali zochuruka momwe iye AMADANA ndikuyalutsidwa, komabe, zikuwonekera pamaso pathu pomwe ndipo ambiri akuchoka.

“Pa chiyambi panali” [Osonkhana ati, “Mawu”—Mkonzi.] “ndipo Mawu anali ndi” [“Mulungu,”] “Ndipo Mawu anali” [“Mulungu.”] “Ndipo Mawu anapangidwa thupi ndipo anadzakhala pakati pathu.” Ndi kulondola uko? Tsopano ife tikuwaona Mawu olonjezedwa omwewo, a Luka, a Malaki, malonjezo onse awa kuyambira lero, akupangidwa thupi, akukhala pakati pa ife, amene ife tinawamva ndi makutu athu; tsopano ife tikumuwona Iye (ndi maso athu) akutanthauzira Mawu Ake Omwe, ife sitikusowa kutanthauzira kulikonse kwa munthu. O mpingo wa Mulungu Wamoyo! pano ndi pa lamya! dzukani mwamsanga, nthawi isanathe!

Tsegulani mitima yanu ndi kumva zimene Mulungu wanena kwa inu, mipingo yake yonse. Tsopano ife tikumuwona IYE, ndi maso athu, AKUTANTHAWUZILA MAWU AKE OMWE. Sitikufuna kutanthauzira kulikonse kwa munthu!! DZUKANI NTHAWI ISANATHE!!

Tamva za zinthu izi moyo wathu wonse zimene zikanati zidzachitike mu nthawi yotsiriza. Tsopano tikuwona ndi maso athu zikuchitika.

Iye anatiuza ife, pali NJIRA IMODZI YOKHA, IYO NDI NJIRA YOPEREKEDWA YA MULUNGU IYE ANAPANGIRA MKWATIBWI WAKE. MUYENERA KUKHALA NDI LIWU LA MULUNGU PA TEPI.

Ndikuitana dziko kuti libwere kudzalumikizana nafe Lamlungu pa 12:00 p.m., nthawi ya ku Jeffersonville, ndi kumva Njira yoperekedwa ndi Mulungu ya lero. Ndiye inunso mukhoza kunena kuti, “Ndamva za Inu, koma tsopano ndikukuonani inu”.

M’bale. Joseph Branham

Uthenga: 65-1127E Ine Ndakhala Ndikumva Koma Tsopano Ine Ndawona

Malemba

Genesis 17
Eksodo 14:13-16
Yobu chaputala 14 ndi 42:1-5
Amosi 3:7
Marko 11:22-26 ndi 14:3-9
Luka 17:28-30

25-0629 Kuyesera Kuti Umuchitire Mulungu Ntchito Popanda Icho Kukhala Chifuniro Cha Mulungu

Uthenga: 65-1127B Kuyesera Kuti Umuchitire Mulungu Ntchito Popanda Icho Kukhala Chifuniro Cha Mulungu

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mkwatibwi wa Khristu, tiyeni ife tibwere palimodzi Lamlungu 12:00 p.m., nthawi ya ku Jeffersonville, kuti tidzamve 65-1127B Kuyesera Kuti Umuchitire Mulungu Ntchito Popanda Icho Kukhala Chifuniro Cha Mulungu

M’bale. Joseph Branham

25-0622 Ntchito Ndi Chikhulupiriro Chofotokozedwa

Uthenga: 65-1126 Ntchito Ndi Chikhulupiriro Chofotokozedwa

PDF

BranhamTabernacle.org

Okondedwa Mawu Opangidwa Thupi,

Aleluya! Maziko a mitima yathu akonzedwa ndi kumva kwa Mawu ndipo Iwo awululira kwa ife, IFE NDIFE Mkwatibwi waukoma wa Khristu; Mwana wa Mulungu wofunika, waukoma, wopanda tchimo, atayima ndi Mawu a Mkwatibwi angwiro, osaipitsidwa, otsukidwa ndi Madzi a Magazi Ake Omwe.

Ife takhala Mawu owonetseredwa opangidwa thupi, kotero kuti Yesu akhoze kutitengera ife, amene Iye anawakonzeratu asanaikidwe maziko a dziko, kupita ku chifuwa cha Atate.

Dziko likhoza kuwona kuwonetsera kwa Chikhulupiriro chathu pa momwe ife tinali kuchitira, ndi kufotokoza kuti ife tiri nalo Vumbulutso loona lochokera kwa Mulungu la Mawu Ake otsimikiziridwa, ndipo ndife opanda mantha. Sitisamala zomwe dziko lonse likunena kapena kukhulupirira… Sewero la atolankhani ndi njira yoperekedwa ndi Mulungu kwa Mkwatibwi wa Yesu Khristu.

Alipo ambiri amene amati amakhulupirira Uthenga wa nthawi yotsiriza uwu, amakhulupirira kuti Mulungu anatumiza mneneri, amakhulupirira kuti William Marrion Branham anali mtumiki wa mngelo wachisanu ndi chiwiri, amakhulupirira kuti analankhula PAKUTI ATERO AMBUYE, koma SAKUKHULUPIRIRA kuti Liwu ndilo liwu lofunika kwambiri lomwe inu muyenera kulimva. Iwo samakhulupirira kuti iye analankhula Mawu osalephera. Iwo samakhulupirira kusewera matepi mu mipingo yawo.

Zimatanthauza chiyani? ZIKUTANTHAUZA KUTI SIZINAWULULIDWE KWA IWO!

Ndi vumbulutso. Iye waziwulula izo kwa inu mwa chisomo Chake. Si zimene inu munachita. Inu simunadzigwirire nokha ntchito mu chikhulupiriro. Inu mumakhala nacho chikhulupiriro, icho chimaperekedwa kwa inu mwa chisomo cha Mulungu. Ndipo Mulungu amaziwulula izo kwa inu, choncho chikhulupiriro ndi vumbulutso. Ndipo Mpingo wonse wa Mulungu wamangidwa pa vumbulutso.

Mwa CHIKHULUPIRIRO izo zaululidwa kwa ife kuti Uthenga uwu ndi Liwu la Mulungu pa matepi amene ajambulidwa, ndi kusungidwa, kuti azidyetsa ndi kufikitsa ungwiro Mkwatibwi wa Yesu Khristu.

Ndi CHIKHULUPIRIRO chenicheni, chosaipitsidwa mu zomwe Mulungu ananena kuti ndi Choonadi. Ndipo Izo zazikika mu mtima mwathu ndi solo ndipo palibe kanthu koti zisunthe Izo. Icho chikhala pomwepo mpaka mneneri Wake atidziwitse ife kwa Ambuye wathu.

Sitingathe kudzithandiza tokha. Iye anatikonzekeretsa ife kuti tilandire ndi kukhulupirira Izo asanaikidwe maziko a dziko. Iye ankadziwa kuti ife tikanalandira Liwu Lake mu m’badwo uno. Iye anatidziwiratu ndipo anatikonzeratu kuti tilandire.

Ndiye, ntchito zomwe Mzimu Woyera ukuchita lero, mwa masomphenya awa osalephera konse, malonjezo osalephera konse, zizindikiro zonse zautumwi zolonjezedwa mu Baibulo, za Malaki 4, ndi, o, Chivumbulutso 10:7, zonse za izo zikukwaniritsidwa; ndi kutsimikiziridwa mwasayansi, njira ina iliyonseyo. Ndipo ngati ine sindinakuwuzeni inu Choonadi, zinthu izi sizikanati zichitike. Koma ngati ine ndakuwuzani inu Choonadi, izo zimachitira umboni kuti ine ndakuwuzani inu Choonadi. Iye akadali yemweyo, dzulo, lero, ndi kwanthawizonse, ndipo mawonetseredwe a Mzimu Wake akumutengera Mkwatibwi kutali. Lolani chikhulupiriro chimenecho, vumbulutso ligwere mu mtima mwanu, kuti, “Ili ndilo oralo.”

Ili ndilo oralo. Uwu ndi Uthenga. Ili ndi Liwu la Mulungu loyitana Mkwatibwi wa Yesu Khristu. O Mpingo, mulole Ambuye akonzere malo ogona a mtima wanu kuti mukhale nacho Chikhulupiriro ndi kuwulula kwa inu kuti kumva Liwu ili, pa matepi, ndi kumene kudzakhala kungwiro ndi kumugwirizanitsa Mkwatibwi wa Yesu Khristu.

Ine kamodzinso ndikukuitanani inu kuti mubwere kudzatijowina ife Lamlungu pa 12:00 P.M., nthawi ya ku Jeffersonville, kuti mudzatengere CHIKHULUPIRIRO Chanu ku malo apamwamba, ndi kukhala limodzi nafe mu malo akumwamba pamene ife tikumva Liwu la Mulungu likutipanga ife kukonzekera kudza Kwake kwaposachedwapa.

M’bale. Joseph Branham

Chonde khalani mu pemphero kwa ife sabata yamawa pamene tikuyamba kampu yathu yoyamba ya Still Waters.

Uthenga: Ntchito Ndi Chikhulupiriro Chofotokozedwa 65-1126

Malemba oti muwerenge:
Genesis 15:5-6, 22:1-12
Machitidwe 2:17
Aroma 4:1-8, 8:28-34
Aefeso 1:1-5
Yakobo 2:21-23
Yohane 1:26, 6:44-46

25-0615 Chilumikizo Chosawoneka Cha Mkwatibwi Wa Khristu

Uthenga: 65-1125 Chilumikizo Chosawoneka Cha Mkwatibwi Wa Khristu

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mkazi Wosankhidwa wa Mulungu,

Palibe njira yozungulira izo, inu ndinu Jini Lauzimu la Mulungu, chiwonetsero cha zikhumbo za maganizo Ake, ndipo munali mwa Iye asanaikidwe maziko a dziko.

Ife sitingapitirirenso, ndife ofanana ndendende ndi njere yomwe idapita munthaka. Ndife Yesu yemweyo, mu mawonekedwe a Mkwatibwi, ndi mphamvu yomweyo, Mpingo womwewo, Mawu omwewo amoyo ndi akukhala mwa ife kupanga mutu, KUKONZEKERA MKWATULO.

Anatiuza ife kuti talekanitsidwa ku mgwirizano wathu woyamba, ndi imfa yauzimu, ndipo tsopano tabadwanso, kapena takwatiwanso, ku mgwirizano wathu watsopano wauzimu. Osatinso moyo wathu wakale wachithupi ndi zinthu za mdziko, koma wa Moyo Wamuyaya. Nyongolosi yomwe inali mwa ife pachiyambi, yatipeza ife!

Zimatanthauza chiyani? Zikutanthauza kuti bukhu lathu lakale lapita ndi mgwirizano wathu wakale, lasamutsidwa. TSOPANO ili mu “Bukhu Latsopano” la Mulungu; osati bukhu la moyo… ayi, ayi, ayi… koma mu Bukhu la Moyo wa Mwanawankhosa. Chimene Mwanawankhosa anachiombola. Ndi chiphaso chathu chaukwati chimene nyongilodzi yathu yaoyo osatha imagwirizirako.

Mwakonzeka? Apa izo zikubwera. Inu kulibwino mudzitsine nokha ndi kukonzekera kukuwa ndi kufuula ulemerero, aleluya, mulemekezeke Ambuye, ndi migolo iwiri ndi katundu wakumwamba.

“Kodi mukutanthauza kundiuza ine kuti buku langa lakale ndi zolakwa zanga zonse, zolephera zanga zonse …”

Mulungu anachiyika icho mu Nyanja ya Kuyiwala Kwake, ndipo inu simunakhululukidwe kokha, koma inu mwalungamitsidwa…Ulemerero!  “Kulungamitsidwa.”

Ndipo izi zikutanthauza chiyani? Zikutanthauza kuti inu simunachite m’komwe ngakhale pa maso pa Mulungu.  Iwe umayima mwangwiro pamaso pa Mulungu. ULEMERERO!  Yesu, Mawu, anatenga malo anu. Iye anakhala inu, kuti inu, wochimwa wonyansa, mukhoze kukhala Iye, MAWU. Ife ndife MAWU.

Izo zimatipanga ife nyongolodzi Yake yaing’ono yomwe inakonzedweratu kuchokera pachiyambi. Ndife Mawu akubwera pa Mawu, pa Mawu, pa Mawu, pa Mawu, ndipo ife tikubwera mu thunthu lokwanila la Khristu kotero kuti Iye akhoze kubwera kudzatitenga ife kuti tikhale Mkwatibwi Wake.

Kodi chikuchitika ndi chiyani TSOPANO?

Ndi Chilumikizano Chosaoneka Cha Mkwatibwi Wa Khristu kusonkhana mozungulira Mawu, kuchokera kuzungulira dziko.

Ponena izi tsopano, izi zikupita mu fuko lonseli. Mu New York, tsopano ili twente-faifi minitsi pasiti leveni. Kutali uko mu Philadelphia ndi kuzungulira kumeneko, oyera okondedwa awo akhala ali uko akumvetsera, pakali pano, mu mipingo konse kozungulira. Kutali uko, kutali komwe kuzungulira Mexico, kutali uko mu Canada ndi konse kozungulira, kudutsa. Mailosi thuu handiredi, kulikonse mkati mwa dera la North America kuno, pafupifupi, anthu ali kumeneko, akumvetsera pakali pano. Zikwi kuchulukitsa ka zikwi, akumvetsera.

Ndiwo Uthenga wanga kwa inu, Mpingo, inu omwe muli mchilumikizano, chilumikizano chauzimu mwa Mawu,

Iye anati Icho chinali chilumikizano chauzimu cha Khristu ndi Mpingo Wake, ndipo Izo ZIKUCHITIKA PALI PANO. Thupi likukhala Mawu, ndipo Mawu akukhala thupi. Ife tawonetseredwa, ndi kutsimikiziridwa; zomwe Baibulo linanena kuti zidzachitika mu tsiku lino, ndipo Izo zikuchitika tsopano, tsiku ndi tsiku mwa aliyense wa ife.

Mulungu adzakhala ndi Mpingo waukoma. Mkwatibwi Wake woona, wokhulupirika wa Mawu. NDIFE AMAYI WOSANKHIDWA wa Ambuye wathu Yesu Khristu.

Ndi Nthawi Yanji Yino, Bwana?

Ife tiri nalo vumbulutso mu masiku otsiriza ano, la Uthenga wa Ambuye Mulungu kuti usonkhanitse Mkwatibwi Wake palimodzi. Palibe m’badwo wina umene iwo unalonjezedwapo. Izo zinalonjezedwa mu m’badwo uno: Malaki 4, Luka 17:30, Yohane Woyera 14:12, Yoweli 2:38. Malonjezo amenewo ali chimodzimodzi basi monga Yohane M’batizi anadzizindikiritsa yekha mu Lemba.

Ndani anakwaniritsa malemba amenewa?

Mngelo wake wamphamvu wachisanu ndi chiwiri, William Marrion Branham. Iye nthawizonse ankazichita izo mwa dongosolo. Iye ankazichita izo nthawi iliyonse mwa dongosolo. Iye akuchita izo kachiwiri mu tsiku lathu, kuitana ndi kusonkhanitsa Mkwatibwi Wake waukoma mu tsiku lotsiriza mwa mneneri Wake.

Ndi nthawi yaulemerero bwanji yomwe Mkwatibwi ali nayo. Kusonkhana kulikonse kumakulirakulira, kokoma komanso kokoma. Sipanakhalepo nthawi ngati iyi. Zokayikira zonse zatha.

Bwerani mudzajowinane nafe pamene tikumva Mawu olonjezedwa a tsiku lathu akuyankhula, ndi kutiuza ife chomwe ife tiri ndi zomwe zikuchitika mu tsiku lathu.  Chilumikizano Chosaoneka Cha Mkwatibwi Wa Khristu 65-1125.

M’bale. Joseph Branham 

Malemba:

Mateyu Woyera 24:24
Luka Woyera 17:30 / 23:27-31
Yohane Woyera 14:12
Machitidwe 2:38
Aroma 5:1/7:1-6
2 Timoteyo 2:14
1 Yohane 2:15
—Genesis 4:16-17; 25-26
Danieli 5:12
Yoweli 2:28
Malaki 4

25-0608 Namulondola

Uthenga: 62-1014E Namulondola

PDF

BranhamTabernacle.org

Okondedwa gulu la Mkwatibwi

Ndipo tsopano Mulungu nthawizonse wakhala akutumiza anamulondola Ake, Iye nthawizonse sanayambe wakhalapo wopanda namulondola, nthawizonse kudutsa mmibadwo. Mulungu nthawizonse amakhala naye wina amene amamuimirira Iye pa dziko lapansi ili, mu mibadwo yonse.

Mulungu safuna kuti tizidalira kumvetsa kwathu kapena maganizo opangidwa ndi anthu. Ndi chifukwa chake amatumiza Mkwatibwi Wake Mtsogoleri; pakuti ali ndi kunvetsa, pomuka ndi choti achite. Mulungu SANAYAMBE WASINTHAPO dongosolo Lake. Iye sanalepherepo kutumiza Namulondola kwa anthu Ake, koma inu muyenera kumuvomereza Namulondola ameneyo.

Inu muyenera kukhulupirira Mawu aliwonse amene Iye amanena kupyolera mwa Namulondola Wake. Iwe uyenera kupita momwe Namulondola Wake akuti uzipita. Ngati muyamba kumvetsera ndi kukhulupirira mawu ena monga kalozera wanu,inu mudzangotayika.

Yohane Woyera 16 akuti Iye anali ndi zinthu zambiri zoti atiuze ife ndi kutiululira kwa ife, potero Iye amatumiza Mzimu Wake Woyera kuti Utitsogolere ndi kutiuza ife. Iye anati Mzimu Woyera ndiye mneneri wotsogolera wa m’badwo uliwonse. Choncho, aneneri ake anatumidwa kuimira Mzimu Woyera kuti atsogolere Mkwatibwi Wake.

Mzimu Woyera umatumizidwa kuti udzatsogolere mpingo, osati gulu lina la amuna. Mzimu Woyera ndiwo luntha-lonse. Anthu amayamba kumakhuthala, amakhala osayanjanitsika.

Si munthuyo, koma Mzimu Woyera MWA munthu ameneyo. Munthu amene anamusankha kuti adziyimire yekha ndi kukhala mtsogoleri wathu wapadziko lapansi amene amatsogoleredwa ndi Mtsogoleri wathu wa Kumwamba. Mawu amatiuza ife kuti tiyenera kumutsatira Namulondola ameneyo. Ziribe kanthu zomwe timaganiza, zomwe zikuwoneka ngati zomveka, kapena zomwe munthu wina anganene, sitiyenera kugawa izi, wotsogolera ndi mmodzi yekha.

Mulungu amatumiza Namulondola, ndipo Mulungu amafuna kuti inu muzikumbukira kuti ameneyo ndi Namulondola Wake woikidwapo.

Mtsogoleri wathu mneneri wasankhidwa ndi Mulungu kuti alankhule Mawu Ake. Mawu ake NDI MAWU A MULUNGU. Mtsogoleri wa mneneri, ndipo iye yekha, ali nako kutanthauzira Kwauzimu kwa Mawu. Mulungu analankhula Mawu Ake kwa iye mulomo kwa khutu. Chifukwa chake, simungathe kutsutsa, kusintha, kapena kulingalira Mawu a Mtsogoleri wanu.

Inu muyenera kumutsatira Iye, ndipo Iye yekha. Ngati simutero, mudzatayika. Kumbukirani, pamene musiya Iye, Wotsogolera wosankhidwa ndi Mulungu, mumakhala nokha, kotero ife tikufuna kukhala pafupi ndi namulondola yemwe Iye anamusankha, ndi kumva ndi kumvera Mawu aliwonse amene Iye amanena kupyolera mwa iye.

Mtsogoleri wathu watiphunzitsa kuti chipangano chakale chinali mthunzi wa chipangano chatsopano.

Pamene Aisrayeli anachoka ku Igupto kupita ku dziko lolonjezedwa, pa Eksodo 13:21 , Mulungu anadziŵa kuti iwo anali asanayendepo mwanjira imeneyo. Anali ma mailosi makumi anayi okha, komabe iwo ankasowa chinachake choti apite nawo. Iwo anataya njira yawo. Kotero Iye, Mulungu, anawatumizira iwo Mtsogoleri. Eksodo 13:21, chinachake chonga chonchi, “Ine ndikutumiza Mngelo Wanga patsogolo panu, Lawi la Moto, kuti likusungeni inu panjira,” kuti likawalondolere iwo ku dziko lolonjezedwa ili. Ndipo ana a Israeli ankatsatira Namulondola uja, Lawi la Moto (usiku), Mtambo usana. Pamene Iwo anaima, iwo anaima. Pamene Iwo adayenda, adayenda. Ndipo pamene Iye anawafikitsa iwo kufupi ndi dziko, ndipo iwo sanali oyenera kuti awoloke, Iye anawatsogolera iwo kubwerera ku chipululu kachiwiri.

Iye anati umenewo ndi mpingo lero. Ife tikanapita kale tikadangodzikonza tokha ndi kukhala mu dongosolo, koma Iye anachita kutitsogolera ife kuzungulira ndi kuzungulira ndi kuzungulira.

Iwo anali oti angotsatira wotsogolera wawo pamene IYE AMATSATIRA ndi kumva kuchokera ku Lawi la Moto. Iye anawauza iwo zimene Mulungu ananena ndipo iwo anayenera kumvera Mawu aliwonse amene iye ananena. Iye anali Liwu la Namulondola. Koma anafunsa ndi kukangana ndi wotsogolera woikidwa ndi Mulungu, motero anayendayenda m’chipululu kwa zaka makumi anayi.

Panali atumiki ambiri m’masiku a Mose. Mulungu anawasankha kuti athandize anthu, monganso Mose sakanatha kuchita zonsezi. Koma udindo wawo unali kuwalozera anthu ku zimene Mose ananena. Baibulo silimanena chirichonse chimene amuna amenewo ananena, ilo limangoti zimene Mose ananena kuti ndi Mawu kuti azitsogolera anthu.

Pamene Mulungu anamuchotsa Mose pamalopo, Yoswa anadzozedwa kuti azitsogolera anthu, zomwe zikuimira Mzimu Woyera lero. Yoswa sanalalikire china chatsopano, komanso sanayese kutenga malo a Mose, komanso sanayese kutanthauzira zomwe wotsogolera ananena; iye anangowerenga zimene Mose ananena ndi kuwauza anthu, “Khalani ndi Mawu. Anangowerenga zimene Mose ananena.

Ndi mtundu wangwiro bwanji wa lero. Mulungu anamutsimikizira Mose ndi Lawi la Moto. Mneneri wathu anatsimikiziridwa ndi Lawi la Moto lomwelo. Mawu amene Mose analankhula anali Mawu a Mulungu ndipo anaikidwa mu Likasa.

Pamene Mose anachotsedwapo, Yoswa anadzozedwa kutsogolera anthu mwa kusunga Mawu amene Mose analankhula pamaso pawo. Iye anawauza iwo kuti akhulupirire ndi kukhala ndi Mawu aliwonse amene kalozera wa Mulungu analankhula.

Yoswa nthaŵi zonse ankaŵerenga zimene Mose analemba Mawu ndi Mawu m’mipukutu. Iye anayika Mawu pamaso pawo nthawizonse. Mawu a tsiku lathu sanalembedwe, koma Iwo anajambulidwa kotero kuti Mzimu Woyera ukhoze kukhala ndi Mkwatibwi Wake kumva Mawu pa Mawu chimene Iye analankhula, mwa Kukanikiza kusewera.

Mulungu sasintha dongosolo Lake. Iye ndi Namulondola wathu. Liwu Lake ndi lomwe likutsogolera ndi kugwirizanitsa Mkwatibwi Wake lero. Ife timangofuna kumva Liwu la Namulondola wathu pamene Ilo limatitsogolera ife ndi Lawi la Moto. Ndi chilumikizano chosaoneka ndi maso cha Mkwatibwi wa Khristu. Ife timalidziwa Liwu Lake.

Pamene namulondola wathu abwera pa guwa, Mzimu Woyera umamukhudza iye ndipo Iwo sulinso iye, koma Namulondola wathu. Iye akukweza mutu wake m’mwamba ndi kufuula, “Atero Ambuye, Atero Ambuye, Atero Ambuye! Ndipo membala aliyense wa Mkwatibwi wa Khristu kuzungulira dziko amabwera kumene kwa iye. Chifukwa chiyani? IFE TIMAMUDZIWA MTSOGOLERI WATHU MMENE IYE AMAYANKHULIRA.

Mtsogoleri Wathu = Mawu
Mawu = Amadza kwa mneneri
Mneneri = Mulungu womasulira yekha waumulungu; Mtsogoleri wake wapadziko lapansi.

58 Muzikhala kumbuyo kwa Mawu! O, inde, bwana! Muzikhala ndi Namulondola ameneyo. Muzikhala kumbuyo komwe kwa Iye. Musamapite kutsogolo kwa Iye, inu muzikhala kumbuyo kwa Iye. Muzimulola Iye kuti azikutsogolerani inu, osati inu muzimutsogolera Iye. Inu muzimulola Iye kuti azipita.

Ngati inu simukufuna kuti mutayike, bwerani mudzamvetsere kwa Namulondola wathu pamene Iye akuyankhula kupyolera mu kalozera Wake woikidwa pa dziko Lamlungu lino pa 12:00 p.M., nthawi ya ku Jeffersonville.

M’bale. Joseph Branham

Uthenga:
62-1014E – Namulondola

Malemba:
Marko 16:15-18
Yohane 1:1/16:7-15
Machitidwe 2:38
Aefeso 4:11-13; 4:30
Ahebri 4:12
2 Petulo 1:21
Eksodo 13:21