All posts by admin5

24-1229 Chibvumbulutso, Mutu Foro Gawo I

Uthenga: 60-1231 Chibvumbulutso, Mutu Foro Gawo I

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Oyera Ovala Mwinjiro Woyera,

Tikamamva Liwu la Mulungu likuyankhula nafe, chinachake chimachitika mkati mwa moyo wathu.  Thupi lathu lonse limasinthidwa ndipo dziko lotizungulira likuwoneka kuti likutha. 

Kodi munthu angakhoze bwanji kufotokoza zomwe zikuchitika mu mitima yathu, malingaliro athu, ndi moyo wathu, pamene Liwu la Mulungu livundukula Mawu Ake ndi Uthenga uliwonse umene timamva?

Monga mneneri wathu, timamva kuti takwatulidwira kumwamba kwachitatu ndipo mzimu wathu ukuwoneka kuti ukuchoka mu thupi lachivundi ili. Palibe mawu ofotokozera zomwe timamva pamene Mulungu akutiululira Mawu ake kuposa kale. 

Yohane anaikidwa pa chisumbu cha Patmo ndipo anapemphedwa kuti alembe zimene anaona ndi kuziika mu bukhu lotchedwa Chivumbulutso, kotero izo zikanadzapita kupyola mu mibadwo. Zinsinsi zimenezo zakhala zobisika mpaka zidaululidwa kwa ife kupyolera mwa mthenga Wake wosankhidwa wa 7.  

Ndiye Yohane anamva Liwu lomwelo pamwamba pa iye ndipo anakwatulidwira kumwamba kwachitatu. Liwu lija linamuwonetsa iye mibadwo ya mpingo, kudza kwa Ayuda, kutsanulidwa kwa miliri, Mkwatulo, Kudza kachiwiri, Zakachikwi, ndi Kwawo Kwamuyaya kwa opulumutsidwa Ake. Iye anamutengera iye mmwamba ndipo anabwereza chinthu chonsecho kwa Yohane monga Iye anati Iye akanadzachita. 

Koma kodi Yohane anaona ndani pamene anaona kubwerezako? Palibe amene amadziwa mpaka lero.  

Chinthu choyamba chimene anaona pakubwera chinali Mose. Iye anaimira oyera mtima akufa amene adzaukitsidwa; mibadwo isanu ndi umodzi yonse yomwe inagona.
Koma si Mose yekha amene anaima pamenepo, komanso Eliya anali pamenepo. 

Kodi Eliya amene anali kuyima anali ndani? 

Koma Eliya anali kumeneko; m’thenga wa tsiku lotsiriza, ndi gulu lake, la osandulika, okwatulidwa.

ULEMELERO…HALELUYA…Kodi Yohane adamuwona atayimapo ndani? 

Osati wina koma mthenga wa mngelo wa 7 wa Mulungu, William Marrion Branham, ndi GULU LAKE LA OSANDULIKA, OKWATULIDWA… ALIYENSE WA IFE!!

Eliya ankayimira oyeramtima akufa…Ine ndikutanthauza Mose, ndi kuwukitsidwa. Eliya ankayimira gulu losandulika. Kumbukirani, Mose anali woyamba, ndipo kenako Eliya. Eliya anali woti adzakhale mthenga wa tsiku lotsiriza, kuti ndi iye ndi gulu lake kukanadzabwera chiwukitsiro…kukanadzabwera…chabwino, ukanadzabwera Mkwatulo, ine ndikutanthauza. Mose anabweretsa chiwukitsiro ndipo Eliya anabweretsa gulu Lokwatulidwa. Ndipo, pamenepo, onse a iwo anayimiriridwa pomwepo.

Lankhulani za kuvundukula, kuwulula, ndi Chivumbulutso. 

Apa Iwo uli! Ife tiri nawo Iwo kumene ndi ife tsopano, Mzimu Woyera, Yesu Khristu, yemweyo dzulo, lero, ndi nthawizonse. Ndinu…Iwo ukulalikira kwa inu, Iwo ukukuphunzitsani inu, Iwo ukuyesera kuti ukufikitseni inu kuti muwone chimene chiri cholondola ndi cholakwika. Ndi Mzimu Woyera Mwiniwake ukuyankhula kupyolera mu milomo ya munthu, ukugwira ntchito pakati pa anthu, kuyesa kusonyeza chifundo ndi chisomo.

Ndife Oyera Ovala Mwinjiro Woyera amene mngelo wake anawaona akuchokera ku dziko lonse lapansi kudzadya Mkate wa Moyo. Tili pa kutomeledwa ndipo wokwatitsidwa ndi Iye ndipo tamva kupsompsona kwa Iye kwa chikwati mu mtima mwathu. Ife tinadzilonjeza tokha kwa Iye, ndi ku Liwu Lake lokha. Tilibe, ndipo sitidzadzidetsa ndi mawu ena aliwonse.

Mkwatibwi akukonzekera kukwera mmwamba monga Yohane anachitira; mu Kukhalapo kwa Mulungu. Tidzakwatulidwa pa Mkwatulo wa Mpingo. Momwe izo zimangozungulira moyo wathu! 

Kodi Iye atiululira chiyani motsatira? 

Ziweruzo; mwala wa sardine, ndi chimene umaimira; idachita gawo lotani. Yaspi, ndi miyala yonse yosiyana. Iye adzazitenga zonse izi mmusi kupyola mu Ezekieli, kubwerera ku Genesis, kubwerera ku Chivumbulutso, kubwera mmusi pakati pa Baibulo, kuzimangiriza izo palimodzi; miyala yonseyi ndi mitundu yosiyanasiyana.

Ndi Mzimu Woyera womwewo, Mulungu yemweyo, kusonyeza zizindikiro zomwezo, zodabwitsa zomwezo, kuchita chinthu chomwecho basi monga Iye analonjezera. Ndi Mkwatibwi wa Yesu Khristu akudzikonzekeretsa Yekha pakumva Liwu Lake.

Ife tikukulandirani inu kuti mulumikizane nafe pamene ife tikulowa mu malo ammwambamwamba pa 12:00 p.M., nthawi ya Jeffersonville, kuti tidzamve Eliya, mthenga wa Mulungu mu m’badwo wotsiriza uno, akuwulula zinsinsi zimene zakhala zobisika mu mibadwo yonse.

M’bale. Joseph Branham

Uthenga:  60-1231 Chivumbulutso,Mutu Foro Gawo I 

Chonde kumbukirani Uthenga wathu wa Chaka Chatsopano, Lachiwiri usiku: Mpikisano 62-1231. Palibe njira yabwinoko yoyambira Chaka Chatsopano.

24-1222 Mphatso Yokulungidwa ya Mulungu

Uthenga: 60-1225 Mphatso Yokulungidwa ya Mulungu

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mkazi Wa JEZU,

O Mwanawankhosa wa Mulungu, Inu ndinu Mphatso yayikulu yokulungidwa ya Mulungu ku dziko. Inu mwatipatsa ife Mphatso yaikulu kwambiri imene inayamba yaperekedwapo, Inu eni. Inu musanalenge nyenyezi yoyamba, Inu musanalenge dziko lapansi, mwezi, mphavu ya dzuwa, Inu munatidziwa ife ndi kutisankha ife kukhala mkwatibwi wanu

Pamene Inu munatiwona ife pamenepo, Inu munatikonda ife. Ife tinali mnofu wa mnofu Wanu, fupa la fupa Lanu; ife tinali gawo la Inu. Momwe Inu munatikondera ife ndi kufuna kuyanjana nafe. Munafuna kugawana nafe Moyo Wanu Wamuyaya. Kenako Tidadziwa pamenepo, tidzakhala Anu m’kazi wa JEZU.

Inu munawona kuti ife tidzalephera, kotero Inu munayenera kutipatsa njira yotibwezeretsa ife . Tinali otayika komanso opanda chiyembekezo. Panali njira imodzi yokha, Munayenera kukhala “Chilengedwe Chatsopano”. Mulungu ndi munthu anayenera kukhala Mmodzi. Inu munayenera kuti mukhale ife, kuti ife tikhoze kukhala Inu. Chotero, Inu munaika dongosolo lanu lalikulu zaka zikwi zapitazo m’munda wa Edeni.

Inu mwakhala olakalaka kwambiri kukhala nafe, Mkwatibwi Wanu wangwiro wa Mawu, koma Inu munadziwa poyamba kuti Inu munayenera kutibwezeretsa ife ku zonse zomwe zinatayika pachiyambi. Munadikirira ndikudikirira ndi kudikirira mpaka kufikila tsiku lino kuti mumalize dongosolo Lanu.

Tsiku lafika. Kagulu kakang’ono kamene mudakawona pachiyambi kali pano. Wokondedwa wanu yemwe amakukondani Inu ndi Mawu Anu kuposa china chilichonse.

Inali nthawi yoti Inu mubwere ndi kudziulula Nokha mu thupi la umunthu monga Inu munachitira ndi Abrahamu, ndipo monga Inu munachitira pamene Inu munakhala Chirengedwe chatsopano. Momwe Inu munali kufunitsitsa za tsiku lino kotero kuti Inu mukhoze kuwulula kwa ife zinsinsi Zanu zonse zazikulu zimene zinali zobisika kuchokera ku maziko a dziko.

Inu mumanyadira kwambiri Mkwatibwi Wanu. Momwe Inu mumakondera kumuwonetsera Iye ndi kumuuza Satana, “Ziribe kanthu zomwe iwe ungayese kuchita kwa iwo, iwo sadzasuntha; iwo sadzanyengerera pa Mawu Anga, Liwu Langa. Iwo ali MKWATIBWI WANGA WA MAWU Angwiro.” Iwo ndi okongola kwambiri kwa Ine. Tangoyang’anani pa iwo! Kupyolera mu mayeso awo onse ndi mayesero, iwo amakhala okhulupirika ku Mawu Anga. ndidzawapatsa mphatso yosatha. Zonse zomwe ndili, ndipereka kwa iwo. TIDZAKHALA AMODZI.

Zonse Zomwe tinganene n’zakuti: “JEZU, TIMAKUKONDANI. Tiloleni ife tikulandireni Inu munyumba mwathu. Tiloleni ife tikudzozeni Inu ndi kusambitsani mapazi anu ndi misozi yathu ndi kuwapsyopsyona iwo. Tifuna Tikuuzeni momwe timakukonderani Inu.”

Zonse zomwe ife tili, tikupereka kwa Inu JEZU. Imeneyo ndiyo mphatso yathu kwa Inu JEZU. Timakukondani. Timakukondani Inu. Ife tikukupembedzani Inu.

Ine ndikukuitanani aliyense wa inu kuti adzakhale nafe Lamlungu pa 12:00 P.M., nthawi yaku Jeffersonville, ndi kumulandira JEZU munyumba mwanu, mu mpingo wanu, mu galimoto yanu, kulikonse kumene inu mungakhale, ndi kulandira Mphatso yaikulu kwambiri imene inayamba yapatsidwapo kwa munthu; Mulungu Mwiniwake akuyankhula ndi kuyanjana ndi inu.

M’bale. Joseph Branham

60-1225 Mphatso Yokulungidwa ya Mulungu

CHIDZIWITSO CHAPADERA

Wokondedwa Mkwatibwi,

Ambuye wayika pamtima wanga kukhala ndi Uthenga Wapadera ndi Utumiki wa Mgonero pa Madzulo a Chaka Chatsopano kachiwiri chaka chino. Ndi chinthu chachikulu chiti chimene tingachite, abwenzi, kuposa kumva Liwu la Mulungu likulankhula kwa ife, kutenga nawo mbali pa Mgonero wa Ambuye, ndi kuperekanso miyoyo yathu ku utumiki Wake pa kulowa mu m’Chaka Chatsopano. Idzakhala nthawi yopatulika bwanji kutsekera dziko kunja, ndi kulumikizana ndi Mkwatibwi pa kusonkhana kwapadera kumeneku mu Mawu, pamene tikunena kuchokera mu mitima yathu, “Ambuye, tikhululukireni ife zolakwa zathu zonse zomwe takhala tikuchita chaka chonse; tsopano tikuyandikira kwa Inu, ndikufunsani ngati mudzatigwira dzanja ndi kutitsogolera chaka chomwe chikubwerachi. Mulole ife tikutumikireni Inu kuposa kale lonse, ndipo ngati icho chiri mu Chifuniro Chanu Chaumulungu, mulole icho chikhale chaka cha Mkwatulo waukulu umene uti uchitike. Ambuye, ife tikungofuna kuti tipite Kwathu kukakhala ndi Inu mu Muyaya.” Ine Sindili onyalanyaza kudikira kusonkhana mozungulira Mpando wachifumu Wake ku msonkhano wapadera wodziperekanso uwu, alemekezeke Yehova.

Kwa okhulupilira okhala mu dera la Jeffersonville, Ine ndikufuna kudzayamba tepi nthawi ya 7:00 pm pa nthawi ya kwathu kuno. Uthenga wonse ndi Mgonero udzakhala pa Wailesi ya Liwu panthawiyo, monga tinachitira m’mbuyomu. Tidzakhala ndi mapaketi a vinyo a Mgonero omwe adzapezeke Lachitatu, pa Disembala 18, kuyambira 1:00 – 5:00 pm, kuti mudzawatengere ku nyumba ya YFYC.

Kwa inu amene mumakhala kunja kwa dera la Jeffersonville, chonde khalani ndi chiyanjano chapadera chimenechi panthawi yomwe ndi yabwino kwa inu kwanuko. Tidzakhala nayo linki yotengera Uthenga ndi Chiyanjano cha Mgonero posachedwapa.

Pamene tikuyandikira Tchuthi cha Khrisimasi, ndikufuna ndikufunireni inu ndi banja lanu Nyengo ya Tchuthi YABWINO NDI YOTETEZEKA, ndi Khrisimasi yabwino, yodzaza ndi chisangalalo cha Ambuye Yesu woukitsidwayo… LIWU.

Mulungu akudalitseni,

M’bale Joseph

Gwero: https://branhamtabernacle.org/en/bt/F6/110067

24-1218 Mau Osazindikirika

Wokondedwa Mkwatibwi Wa Mpingo Wa Pakhomo,

Tiyeni tonse tisonkhane pamodzi ndikunvetsera uthenga 60-1218-Mau Osazindikirika, Lamlungu lino pa 12:00PM,
Nthawi ya ku Jeffersonville.

M’bale. Joseph Branham.

24-1208 M’badwo Wa Mpingo Wa Laodikaya

Uthenga: 60-1211E M’badwo Wa Mpingo Wa Laodikaya

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Osankhidwa,

Taonani, ndaima pakhomo, ndi kugogoda: ngati wina amva mau Anga, ndikutsegula pakhomo, ndidzalowa mwa iye, ndipo ndidzadya naye, ndi iye ndi Ine.

Utumiki, tsegulani makomo anu kwa mngelo wa Mulungu nthawi isanathe. Ikani Liwu la Mulungu libweleleso mu maguwa anu posewera matepi. Ndi Liwu lokhalo lotsimikiziridwa la Mulungu la tsiku lathu ndi Mawu osalephera. Ndi Mau okhawo omwe ali ndi PAKUTI ATERO AMBUYE. Ndi Liwu lokhalo Mkwatibwi aliyense angakhoze kunena AMEN kwa iye.

Ndi m’badwo waukulu kuposa nthawi zonse. Yesu akutipatsa kufotokoza kwa Iye mwini pamene masiku a chisomo chake akutha. Nthawi yafika kumapeto. Iye waulula makhalidwe Ake omwe kwa ife mu m’badwo wotsiriza uno. Watipatsa kuyang’ana komaliza pa Umulungu Wake Wachisomo ndi wapamwamba. M’badwo uwu uli vumbulutso la mwala wa pamutu la Iye mwini.

Mulungu anabwera mu m’badwo wa Laodikaya uwu ndipo anayankhula kupyolera mu thupi la munthu. Liwu Lake linalembedwa ndi kusungidwa kuti litsogolere ndi kupangitsa ungwiro Mkwatibwi wa Mawu Ake. Palibenso Liwu lina limene lingakhoze kupangitsa Mkwatibwi Wake kukhala wangwiro koma Liwu Lake Lomwe.

Mu m’badwo wotsiriza uno, Liwu Lake pa matepi layikidwa pambali; latulutsidwa kunja kwa mipingo. Iwo sasewera matepi. Chotero Mulungu akuti, “Ine ndikutsutsana nanu nonse. Ine ndidzakulavula iwe mkamwa Mwanga. Awa ndi mathero.

“Pa mibadwo isanu ndi iwiri mwa mibadwo isanu ndi iwiri, sindinawone kalikonse koma anthu olemekeza mawu awo omwe kuposa Anga. Chotero pa mapeto a m’badwo uwu Ine ndikulavula inu kutuluka mkamwa Mwanga. Zonse zatha. Ndilankhula inde cha bwino. Inde, ndili pano pakati pa Mpingo. Ameni wa Mulungu, wokhulupirika ndi woona adzadziulula Yekha ndipo izo zikhala NDI MNENERI WANGA.”

Monga mmene zinalili poyamba, iwo akuyenda moona mtima n’kukhala mmene anachitira makolo awo akale m’masiku a Ahabu. Anali mazana anai a iwo, ndipo onsewo anali mu m’gwirizano; ndipo mwa iwo onse kunena chinthu chomwecho, iwo anapusitsa anthu. Koma mneneri MMODZI, MMODZI YEKHA, anali wolondola ndipo ena onse olakwa chifukwa Mulungu anali atapereka vumbulutso kwa MMODZI YEKHA.

Izi sizikunena kuti mautumiki onse ndi abodza ndi kupusitsa anthu. Komanso sindikunena kuti munthu amene ali ndi mayitanidwe otumikira sangathe kulalikira kapena kuphunzitsa. Ine ndikunena kuti Utumiki wofutukuka usanu WOWONA udzayika MATEPI, Liwu la Mulungu kwa Mkwatibwi, ngati Liwu lofunika kwambiri lomwe inu MUYENERA KUMVA. Liwu la pa matepi liri Liwu LOKHALA limene latsimikiziridwa ndi Mulungu Mwiniwake kuti liri PAKUTI ATERO AMBUYE.

Chenjerani ndi aneneri onyenga, pakuti iwo ndi mimbulu yolusa.

Kodi mungadziwe bwanji njira yolondola ya lero? Pali kusiyana koteroko pakati pa okhulupirira. Gulu limodzi la anthu limati utumiki wofutukuka usanu udzachititsa Mkwatibwi kukhala wangwiro, pamene ena amati Kusewera matepi basi. Sitiyenera kugawanika; ife tiyenera kuti tigwirizane ngati MKWATIBWI MMODZI. Yankho lolondola ndi liti?

Tiyeni titsegule mitima yathu palimodzi ndi kumva zomwe Mulungu akunena kudzera mwa mneneri Wake kwa Mkwatibwi. Pakuti ife tonse tikuvomereza, kuti M’bale Branham ndi mngelo mthenga Wake wa wachisanu ndi chiwiri.

Pamaziko a khalidwe laumunthu lokha, aliyense amadziwa kuti pamene pali anthu ambiri pali ngakhale malingaliro ogawanika pa mfundo zazing’ono za chiphunzitso chachikulu chimene onse amagwirizira pamodzi. Ndani ndiye amene adzakhala nayo mphamvu ya kusalephera yomwe iti ibwezeretsedwe mu m’badwo wotsiriza uno, pakuti m’badwo wotsiriza uwu ubwereranso ku kuwonetsera Mkwatibwi wa Mawu Oyera? Izo zikutanthauza kuti ife tidzakhala nawo Mawu kamodzinso monga iwo anaperekedwa mwangwiro, ndi kumveka mwangwiro mu masiku a Paulo. Ndikuuzani amene adzakhala nayo. Iye adzakhala mneneri monga wotsimikiziridwa mwathunthu, kapena ngakhale wotsimikiziridwa mwathunthu kuposa momwe analiri mneneri aliyense mu mibadwo yonse kuchokera kwa Enoki mpaka tsiku lino, chifukwa munthu uyu mofunikila adzakhala nawo utumiki wa uneneri wa mwala wapamwamba, ndipo Mulungu adzamuwonetsa iye apo. Iye sadzasowa kuti aziyankhulire yekha, Mulungu adzayankhula mmalo mwa iye ndi liwu la chizindikiro. Ameni.

Chotero, Uthenga uwu wolankhulidwa ndi mthenga Wake unaperekedwa mwangwiro, ndipo umamveka mwangwiro.

Kodi Mulungu ananenanso chiyani china za mngelo Wake wachisanu ndi chiwiri wamthenga ndi Uthenga wake?

  • Adzamvera kwa Mulungu yekha.
  • Adzakhala ndi pakuti “atero Ambuye” ndi kuyankhula m’malo mwa Mulungu.
  • Iye adzakhala kamwa ya Mulungu.
  • IYE, MONGA KUNALEMBEDWA PA Malaki 4:6, ADZABWEZERETSA MITIMA YA ANA KUBWELERA KWA ATATE.
  • Iye adzabwezeretsanso osankhidwa a tsiku lomaliza ndipo adzamva mneneri wotsimikiziridwa akupereka choonadi chenicheni monga momwe zinalili ndi Paulo.
  • Adzabwezeretsa chowonadi monga adali nacho.

Ndiyeno kodi Iye ananena chiyani za ife?

Ndipo iwo osankhidwa pamodzi ndi iye mu tsiku limenelo adzakhala iwo amene moona adzawonetsera Ambuye ndi kukhala Thupi Lake ndi kukhala liwu Lake ndi kuchita ntchito Zake. Aleluya! Kodi inu mukuziwona izo?

Ngati mukadali mu kukaikira kulikonse, funsani Mulungu mwa Mzimu Wake kuti akudzazeni inu ndi kukutsogolerani inu, pakuti Mawu amati, “ OSANKHIDWA KUMENE KOKHA SADZAPUSITSIDWA”. Palibe mwamuna aliyense amene angakunyengeni inu ngati ndinu Mkwatibwi.

Pamene Amethodisti analephera, Mulungu anadzutsa ena ndipo kotero izo zapitirira kupyola mu zaka mpaka mu tsiku lotsiriza ili palinso anthu ena mu dziko, amene pansi pa mthenga wawo adzakhala liwu lotsiriza ku m’badwo wotsiriza.

Inde bwana. Mpingo sulinso “choyankhulira” cha Mulungu. Iyemwini ali kamwa payekha. Chotero Mulungu akutembenukira pa iye. Iye adzaphatikizana ndi iye kupyolera mwa mneneri ndi mkwatibwi, pakuti liwu la Mulungu lidzakhala mwa iye. Inde, chifukwa anena m’mutu wotsiriza wa Chivumbulutso vesi 17, “Mzimu ndi mkwatibwi anena, Idzani.” Kamodzinso dziko lidzamva molunjika kuchokera kwa Mulungu monga pa zinalili pa Pentekosite; koma ndithudi Mkwatibwi wa Mawu uyo ​​adzakanidwa monga zinalili mu m’badwo woyamba.

Mkwatibwi ali nalo liwu, koma ilo lidzangonena zomwe ziri pa matepi. Pakuti Liwu limenelo ndi LOLUNJIKA KUCHOKERA KWA MULUNGU, motero silikusowa kutanthauzira monga linaperekedwa mwangwiro ndipo limamveka mwangwiro.

Bwerani mudzajowine nafe Lamulungu lino pa 12:00 P.M., nthawi yaku Jeffersonville, pamene ife tikumva Liwu lija likuwululira kwa ife: M’badwo wa Mpingo wa Laodikaya 60-1211E. 

Mbale. Joseph Branham

24-1201 Anamwali Khumi, Ndi Ayuda Handirede Ndi Forte-Foro Sauzande

Uthenga: 60-1211M Anamwali Khumi, Ndi Ayuda Handirede Ndi Forte-Foro Sauzande

PDF

BranhamTabernacle.org

M’mawa Wabwino Abwenzi

Sizinayambe zachitikapo mu mbiri yakale ya dziko pamene M’kwatibwi wa Khristu wochokera kuzungulira dziko anakhoza kulumikizidwa palimodzi mu mgwirizano umodzi, pamene mkokomo wochokera Kumwamba, Liwu lomwe la Mulungu, likanakhoza kubwera mothamanga mkati. 

Malemba akukwaniritsidwa.  Ndi nthawi yachilumikizano chizindikiro cha Mbewu.  Chilumikizano chosawoneka cha Mkwatibwi wa Khristu chikuchitika pamene ife tikukhala pamaso pa Mwana wamwamuna, kucha, kudzikonzekeretsa Yekha pakumva Liwu lomwelo la Mulungu. 

Ife tikupangidwa angwiro ndi utumiki Wake wofutukuka pasanu.

Ndi angati amakhulupirira kuti mphatso ndi maitanidwe ziri zopanda kulapa?  Baibulo linati pali mphatso zisanu mu mpingo.  Mulungu anaika mu mpingo Atumwi, kapena amishonare, atumwi, aneneri, aphunzitsi, avangeli, abusa. 

  • Mlaliki: Ine ndingapite kumusi  mumsewu uko. Ndiye  winawake akanati, “Kodi ndiwe mlaliki?”  Ine ndikanati, “Inde bwana.  Inde, ndine mlaliki.” 
  • Mphunzitsi: Ndipo tsopano chifukwa chimene ine sindinayambe ndalalikira mmawa uno, chinali chifukwa, ine ndinaganiza, pophunzitsa, ife tikanamvetsa izo bwinoko kuposa kungotenga mutu ndi kuwulumpha iwo.  Ife tikanangophunzitsa izo.
  • Mtumwi: Mawu akuti “mmishonale” amatanthauza “m’modzi wotumizidwa.”  “Mtumwi” amatanthauza “mmodzi wotumidwa.”  Mmishonale ndi mtumwi.  Ine—ine, ndine mmishonare, monga inu mukudziwa, ndimachita uvangeli, ntchito ya umishonare, pafupi kasanu ndi kawiri kutsidya kwa nyanja, kuzungulira dziko. 
  • Mneneri: Kodi mukundikhulupirira kuti ndine mneneri wa Mulungu?  Kenako pita ukachite zimene ndakuuza. 
  • Abusa: Mukudziwa chimene ndakuchitirani inu?  Inu mumanditcha ine m’busa wanu, ndipo inu mukunena bwino, pakuti chotero ine ndiri. 

Ndipo ine ndinawawona mamilioni awo atayima pamenepo, ine ndinati, “Kodi onsewo ndi a Branham?”  Anati, “Ayi.”  Anati, “Iwo ndi otembenuka anu.”  Ndipo ine ndinati, ine—ine ndinati, “Ine ndikufuna kumuwona Yesu.”   Iye anati, “Ayi.  Idzakhala nthawi Iye asanabwerebe.  Koma Iye adzabwera kwa inu poyamba ndipo inu mudzaweruzidwa ndi Mawu amene inu munawalalikira, 

Ndiye tonse tinakweza manja athu ndi kunenabkuti, “Ife tikupumura pa icho!” 

Chinachake chikukonzekera kuti chichitike.  Chikuchitika ndi chiyani?  Akufa mwa Khristu ayamba kuwuka pozungulira ine.  Ndikumva kusintha kwabwera mthupi langa.  Tsitsi langa la Imvi, lapita.  Yang’anani nkhope yanga … makwinya anga onse atha.  Zopsinja zanga ndi zowawa …. ZAPITA. Maganizo anga ankhawa atha nthawi yomweyo.  Ndasinthidwa mu m’kamphindi, mu m’kuphethira kwa diso.

Kenako tidzayamba kuyang’ana pozungulira ife ndikuwona okondedwa athu.  O mai, pali Amayi ndi Abambo…Ulemelero, mwana wanga wamamuna…mwana wanga wamkazi.  Agogo amuna, Agogo akazi, oh ndinakusowani nonse.  Hei … pali mzanga wakale.  O TAWONANI, ndi M’bale Branham, mneneri wathu, Aleluya!!  Ndi pano.  Zikuchitika! 

Ndiye palimodzi, zonse mwakamodzi, ife tidzakwatudwira kutali kwinakwake mu mlengalenga kuseri kwa dziko lapansi.  Tidzakomana ndi Ambuye panjira Yake yotsika.  Ife tidzayima pamenepo ndi Iye pa mphete za dziko lapansi ndi kuyimba nyimbo za chiwombolo.  Tidzayimba ndi kumuyamika Iye chifukwa cha chisomo Chake chachiwombolo chimene Iye watipatsa ife.

Zonse zomwe zili munkhokwe ndiza Mkwatibwi Wake. Ndi nthawi yanji yomwe ife titi tidzakhale nayo kunthawi zamuyaya wina ndi mzake, ndi Ambuye wathu Yesu.  Mawu achivundi sangakhoze kufotokoza, Ambuye, momwe ife tikumvera mu mitima yathu. 
Ngati inu mukufuna kuti mumumve Iye akukuitanani inu Mkwatibwi Wake, ndi kukuuzani inu momwe izo ziti zidzakhalire ndi Iye, bwerani muzajoinane  nafe Lamulungu lino pa 12:00 P.M., nthawi yaku Jeffersonville, ndipo inu mudzadalitsidwa mopitirira muyeso.

M’bale.  Joseph Branham

60-1211M –  Anamwali Khumi, Ndi Ayuda Handirede Ndi Forte-Foro Sauzande

24-1124 M’badwo Wa Mpingo Wa Filadelfia

Uthenga: 60-1210 M’badwo Wa Mpingo Wa Filadelfia

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mkazi Wa Yesu Khristu,

Kodi Lamulungu lino ligwirizira chiyani kwa Mkwatibwi wa Yesu Khristu? Kodi mchiyani chomwe Mzimu Woyera adzatiwululira ife? Kuzindikira Kwangwiro. Tsopano tidzamvetsetsa bwino lomwe ndi Chivumbulutso, chophiphiritsira chosiyanitsidwa ndi choyimira ndi chinthu ndi mthunzi. Yesu ndiye Mkate weniweni wa Moyo. Iye ali wothunthu wa Iwo. Iye ndi Mulungu Mmodzi. Iye ndi Aheberi 13:8. Iye ali INE NDINE.

Khristu, pakuwonekera mu thupi ndi kukhetsa Magazi Ake omwe, adachotsa machimo athu kamodzi kokha kwamuyaya mwa nsembe ya Iyemwini; chotero Iye tsopano watipanga ife ANGWIRO. Moyo wake womwe uli mwa ife. Mwazi Wake watiyeretsa ife. Mzimu wake umatidzadza ife. Ndi Mikwingwirima Yake yinatichiritsa KALE.
Mawu ake ali mumtima mwathu ndi m’kamwa mwathu. Ali Khristu m’miyoyo yathu ndipo palibe china chilichonse, popeza chilichonse m’miyoyo yathu chinachokamo ndikukukhala chopanda pake, kupatula Iye ndi Mawu Ake.

Mtima wathu udzadzazidwa ndi chimwemwe pamene Iye akutiuza kuti mwa lamulo lake la uzimu, Iye anadziwa ndendende amene adzakhala Mkwatibwi Wake. Momwe Iye anatisankhira ife. Iye anatiyitana ife. Iye anatifera ife. Iye analipira mtengo wa ife ndipo ife ndife ake, ndipo Iye yekha. Amayankhula, ndipo timamvera, chifukwa ndi chisangalalo chathu. Ndife chuma Chake chokhacho ndipo alibe wina koma IFE. Iye ndi Mfumu yathu ya Mafumu ndipo ife ndife ufumu Wake. Ndife chuma chake chamuyaya.

Iye adzatilimbitsa ndi kutiunikira ndi Liwu lake. Adzafotokoza momveka bwino ndikuulula kuti Iye ndiye Khomo la nkhosa. Iye ali zonse Chiyambi ndi Mapeto. Iye ndi Atate, ndi Mwana wa mwamuna, ndi Mzimu Woyera. Iye ali Mmodzi, ndipo ife tiri amodzi ndi Iye ndi mwa Iye.

Adzatiphunzitsa kuleza mtima, monga anachitira Abrahamu, mwa kufotokoza mmene tiyenera kuyembekezera moleza mtima ndi kupirira ngati tikufuna kulandira lonjezo lililonse.

Adzatiwonetsa momveka bwino tsiku lomwe tikukhalamo. Momwe kusuntha kwa matchalitchi kudzalimba kwambiri pazandale, ndi kukakamiza kwa boma kuti onse alowe nawo mwa kutsatira mfundo zokhazikitsidwa ndi kukhala lamulo, kuti pasapezeke anthu kudziwika ngati mipingo pokhapokha ngati pali ulamuliro wachindunji kapena wosalunjika kwa bungwe lawo.
Iye adzawulula kuti ndi angati amene adzapite nawo, akumaganiza kuti akutumikira Mulungu
mu dongosolo la bungwe. Koma Iye amatiuza ife, “Musawope, pakuti Mkwatibwi sadzanyengedwa, ife tidzakhala ndi Mawu Ake, Liwu Lake.

Zidzakhala zolimbikitsa chotani nanga kumva Iye akutiuza kuti: “Gwirani Mofulumira, limbikirani. Osataya mtima, koma valani zida zankhondo zotetenzera zonse za Mulungu, chida chilichonse, mphatso iliyonse yomwe ndakupatsani ili m’manja mwathu. Usataye mtima konse wokondedwa, ingoyang’ana kutsogolo ndi chisangalalo chifukwa udzavekedwa korona ndi Ine, Mfumu yako ya Mafumu ndi Mbuye wa Ambuye, Mwamuna wako. “

Inu ndinu mpingo Wanga woona; kachisi yemweyo wa Mulungu mwa Mzimu Wanga Woyera amene akukhala mwa inu. mudzakhala mizati m’Kacisi watsopano;
maziko omwewo omwe angagwirizanitse mawonekedwe apamwamba. Ine ndidzakuikani inu ngati wogonjetsa limodzi ndi atumwi ndi aneneri, pakuti Ine ndakupatsani inu Vumbulutso la Mawu Anga, la Inemwini.

Iye adzawulula momveka bwino kwa ife kuti maina athu analembedwa mu Bukhu la Moyo wa Mwana wa nkhosa Wake asanayikidwe maziko a dziko. Chotero tidzakhala pamaso pa mpando wake wachifumu usana ndi usiku kumtumikira Iye m’kachisi wake. Ndife chisamaliro chapadera cha Ambuye; ndife Mkwatibwi Wake.

Tidzakhala ndi dzina latsopano potenga dzina lake. Lidzakhala dzina limene lidzapatsidwa kwa ife pamene atitengera kwa Iyemwini. Ife tidzakhala Mkazi Wake Wa Yesu Khristu.

Yerusalemu watsopano akutsika kuchokera kwa Mulungu kuchokera kumwamba, Mkwatibwi wokongoletsedwera Mwamuna wake. Sipadzakhalanso imfa, chisoni, kapena kulira. ndipo sipadzakhalanso chowawitsa, pakuti zoyambazo zapita; Malonjezo onse odabwitsa a Mulungu adzakwaniritsidwa. Kusintha kudzamalizidwa. Mwana wa nkhosa ndi Mkwatibwi Wake adzakhala kwanthawizonse okhazikika mu ungwiro wonse wa Mulungu.

Wokondedwa Mkazi Wa Yesu Khristu, LOTANI ZA IZO. Zidzakhala zodabwitsa kwambiri kuposa momwe mungaganizire.

Ine ndikuyitana aliyense kuti abwere kudzatijowina ife Lamulungu lino pa 12:00 p.m., nthawi ya ku Jeffersonville, pamene Mwamuna wathu, Yesu Khristu, akuyankhula kupyolera mwa mthenga Wake wamphamvu wa mngelo wachisanu ndi chiwiri ndi kutiuza ife zinthu zonse izi.

M’bale. Joseph Branham

Uthenga: M’badwo Wa Mpingo Wa Filadelfia 60-1210

24-1117 M’badwo Wa Mpingo Wa Sarde

Uthenga: 60-1209 M’badwo Wa Mpingo Wa Sarde

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Anthu A Tepi,

Ndife onyadira bwanji kutchedwa “Anthu a Tepi”. Mitima yathu imathamanga ndi chisangalalo mlungu uliwonse podziwa kuti tidzakhala osonkhana Pamodzi padziko lonse lapansi pomva Liwu la Mulungu likuyankhula kwa ife.

Tikudziwa, popanda mthunzi wa chikaiko chimodzi, tili mu Chifuniro changwiro cha Mulungu pakukhala ndi Mawu Ake; kumvetsera ku Liwu Lake mwa njira ya mngelo Wake wamphamvu wamthenga wachisanu ndi chiwiri.

Mtumiki yemwe Iye anamusankha wa tsiku lathu ndi William Marrion Branham. Iye ndiye nyali ya Mulungu pa dziko lapansi, ikuunikira kuunika kwa Mulungu. Iye akuyitana mkwatibwi wosankhidwa Wake wa Mawu Oyera mwa mngelo Wake.

Mwa kuphunzira mosamalitsa kwa Mawu Ake, Iye waululira kwa ife mwa Mzimu Wake Woyera kuti William Marrion Branham ndi mngelo yemwe Iye anamusankha kuti apereke Chivumbulutso Chake ndi Utumiki kwa tsiku lathu. Ife tikuona mngelo Wake, NYENYEZI YATHU, mu dzanja Lake lamanja pamene Iye akumupatsa iye mphamvu Yake kuti awulule Mawu Ake ndi kuitana kunja Mkwatibwi Wake.

Iye watipatsa ife Vumbulutso lathunthu la Iyemwini. Mzimu Woyera kudzizindikiritsa Yekha kwa ife kupyolera mu moyo wa mtumiki Wake wa mngelo wachisanu ndi chiwiri; mngelo amene anamusankha kukhala maso ake a m’tsiku lathu lino.

Momwe mitima yathu imatenthera mkati mwathu pamene Iye amatiuza ife ndi Uthenga uliwonse kuti ndi cholinga Chake kutibweretsera ife kwa Iye mwini; kuti ndife Mkwatibwi wa Mawu Ake.

Iye amakonda kutiuza mobwereza bwereza momwe Iye anatisankhira ife asanaikidwe maziko a dziko MWA IYE. Momwe ife tinadziwidwiratu ndi kukondedwa ndi Iye.

Momwe ife timakondera kumumva Iye akuyankhula ndi kutiuza ife kuti tinawomboledwa ndi Magazi Ake ndipo MKOSATHEKA kubwera mu kutsutsidwa. Sitingakhale konse mu mchiweruzo, chifukwa tchimo silingawerengedwe kwa ife.

Momwe ife titi tidzakhale ndi Iye pamene Iye akutenga mpando Wake wachifumu wapadziko lapansi wa Davide, ndipo ife tikulamulira ndi Iye; monga anachitira kumwamba, ndi mphamvu ndi ulamuliro pa dziko lonse lapansi. Mayeso ndi mayesero a moyo uno adzawoneka ngati opanda pake.

Koma watichenjezanso za mmene tiyenera kusamala. Kuti mu mibadwo yonse mipesa iwiriyo inamera mbali ndi mbali. Momwe mdani nthawi zonse wakhala ali pafupi kwambiri; wonyenga kwambiri. Ngakhale Yudasi anasankhidwa ndi Mulungu, ndipo anaphunzitsidwa mu choonadi. Anagawana chidziwitso cha zinsinsi. Iye anali ndi utumiki wa mphamvu wopatsidwa kwa iye ndipo iye anachiritsa odwala ndi kutulutsa ziwanda mu Dzina la Yesu. Koma iye sakanakhoza kupita njira yonse.

Inu simungakhoze kupita limodzi ndi gawo chabe la Mawu, inu muyenera kutenga Mawu ONSE. Pali anthu amene amaoneka okhudzidwa ndi zinthu za Mulungu pafupifupi zana limodzi pa zana, koma satero.

Iye anati sikunali kokwanira kuti Iye wadziphatikiza Yekha ndi mpingo wonse, kapena ngakhale ndi utumiki usanu wa Aefeso 4. Iye anatichenjeza ife kuti mu m’badwo uliwonse mpingo umasokera, ndipo si anthu wamba okha komaso gulu la atsogoleri achipembedzo — abusa ali olakwa monganso nkhosa.

Chotero mwa uphungu wotsimikizirika wa chifuniro Chake chomwe, Iye anadzibweretsa Yekha powonekera mu m’badwo wathu monga M’busa Wamkulu mu utumiki wa mthenga Wake wa mngelo wachisanu ndi chiwiri kutsogolera anthu Ake kubwerera ku choonadi ndi mphamvu yochuluka ya choonadi chimenecho.

Iye ali mwa Mthenga Wake ndipo amene angakhale ndi chidzalo cha Mulungu adzatsatira Mtumiki monga Mtumikiyo ali wotsatira wa Ambuye mwa Mawu Ake.

Ine ndikufuna kukhala nacho chidzalo cha Mulungu ndi kutsatira mtumiki Wake. Kotero, kwa ife, aku m’pingo wa Branham , njira yokhayo yotsatirira mtumiki pamene iye akutsatira Ambuye mwa Mawu Ake, ndi KUSINDIKIZA KUSEWERA ndi kumva Liwu Loyera la Mulungu likulankhula kwa ife mawu osalephera.

Sitiyenera kuganiza kapena kuyang’ana zomwe tikumva, timangoyenera Kusindikiza kusewera ndikukhulupirira Mawu aliwonse omwe tikumva.

Ine ndinamumva M’bale Branham akunena mawu otsatirawa molawirira mmawa wina pa wailesi ya liwu. Nditamva Izi, zidabwera mu mtima mwanga kuti umu ndi momwe timamvera tikamati:

TIMANGOSINDIKIZA KUSEWERA NDI KUMVETSEMVERA MA TEPI.

Zinamveka ngati mawu a Chikhulupiriro chathu kwa ine.

Ndicho chifukwa ine ndimakhulupirira mu Uthenga uwu, ndi chifukwa Iwo umachokera ku Mawu a Mulungu. Ndipo chirichonse chakunja kwa Mawu a Mulungu, ine sindimakhulupirira izo. Izo zikhoza kukhala chomwecho, komabe ine ndingokhala ndi zomwe Mulungu ananena, ndiyeno ndidzakhala wotsimikiza kuti ine ndikulondola. Tsopano, Mulungu akhoza kuchita chimene Iye akufuna. Iye ndi Mulungu. Koma bola ngati ine ndikhala ndi Mawu Ake, ndiye ine ndimadziwa kuti izo nzabwino. Ndikukhulupirira zimenezo.

Ulemerero, iye anati izo ndi ZANGWIRO KWAMBIRI. Utumiki wina uliwonse ukhoza kukhala, chifukwa Mulungu akhoza kuchita zomwe Iye akufuna, ndi yemwe Iye akufuna kutero, Iye ndi Mulungu. Koma bola ngati ine ndikhala ndi Mawu Ake, Liwu Lake, Matepi, ndiye ine ndimadziwa kuti izo ndizolondola. Ndikukhulupirira zimenezo.

Ndikudziwa kuti ambiri amawerenga makalata anga ndipo samamvetsetsa zomwe ndikunena komanso zomwe ndimakhulupirira kuti ndi Chifuniro cha Ambuye kwa mpingo wathu. Ndiloleni ndinenenso modzichepetsa monga momwe mneneri ananenera kuti: “Makalata amenewa analembedwera mpingo wanga wokha. Iwo amene akukhumba kuti azitchula kuti Branham Tabernacle ndi mpingo wawo. Omwe AMAFUNA KUDZIWIKA NDI KUTCHEDWA ANTHU A TEPI”.

Ngati simukugwirizana ndi zomwe ndikunena komanso kukhulupirira, zili bwino abale ndi alongo anga. Makalata anga sanalembedwe kwa inu kapena motsutsana ndi inu kapena mipingo yanu. Mpingo wanu ndi woyima pawokha ndipo muyenera kuchita monga momwe mukumverera kuti mukutsogozedwa kuti muchite, koma molingana ndi Mawu, momwemonso kotero Uli wathu, ndipo izi ndi zomwe tikukhulupirira kuti ndi njira yoperekedwa ndi Mulungu kwa ife.

Nonse ndi olandiridwa nthawi zonse kusonkhana nafe Lamlungu lililonse pa 12:00 P.M., nthawi ya Jeffersonville. Sabata ino, Nyenyezi ya Mulungu ya m’badwo wathu, William Marrion Branham, adzakhala kutibweretsera ife Uthenga, 60-1209 M’badwo wa Mpingo wa Sardean.

M’bale. Joseph Branham