All posts by admin5

25-0831 Ukulirira Chiyani? Yankhula!

Uthenga: 63-0714M Ukulirira Chiyani? Yankhula!

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mpingo wa Mulungu,

Mulungu analankhula nati, ““Ine sindigwira ntchito pa dziko lapansi, kupatula kupyolera mwa munthu. Ine—Ine—Ine ndine Mpesa; inu ndinu nthambi. Ndipo ine ndimadzifotokoza kokha Inemwini pamene ine ndingakhoze kupeza munthu M’MODZI. Ndipo Ine ndamusankha iye, William Marrion Branham. Ine ndamutumiza iye kumusi kuti adzaitane Mkwatibwi Wanga. Ine ndidzaika Mau anga mu mkamwa mwake . Mau anga adzakhala Mau ake. Iye adzalankhula Mau anga ndi kumalankhula zokhazo zomwe ine ndimalankhula.

Liwu la Lemba linayankhula kupyolera mu Lawi la Moto ndipo linamuuza iye, “Ine ndakusankha iwe, William Branham. Iwe ndi mwamunayo. Ine ndinakulera iwe kwa cholinga ichi. Ine ndidzakutsimikizira iwe mwa zizindikiro ndi zodabwitsa. Iwe ukupita ku dziko la pansi kuti ukaulule Mawu Anga ndi kukamutsogolera Mkwatibwi Wanga. Mawu Anga ayenera kuti akwaniritsidwe ndi IWE.”

Mneneri wathu ankadziwa kuti anatumidwa ndi cholinga chomwecho kuti aulule zinsinsi zonse za Baibulo ndi kutsogolera Mkwatibwi wa Mulungu ku Dziko Lolonjezedwa. Iye ankadziwa chimene iye ananena, Mulungu akanadzalemekeza ndi kuchikwaniritsa. Ine ndikufuna kuti inu musamaiwale Mawu amenewo. Zimene mneneri wathu ananena, Mulungu azilemekeza, chifukwa Mawu a Mulungu anali mwa William Marrion Branham. Iye ali Liwu la Mulungu kwa dziko.

Iye ankadziwa kuti iye anali mngelo wodzozedwa wa Mulungu. Iye ankadziwa mumtima mwake zonse zimene Mulungu ananena zokhudza iye m’Mawu ake. Zomwe zinkamudetsa nkhawa kwambiri zinali zitachitikadi. Iye anali wodzozedwa ndipo ankadziwa kuti iye anali ndi PAKUTI ATERO AMBUYE. Palibe chimene chikanamuletsa kupita kukalankhula Mawu a Mulungu.

Mulungu anamuuza iye, “Mawu Anga, ndi iweyo, Mtumiki Wanga, muli ofanana.” Iye ankadziwa kuti iye ndi amene anasankhidwa kulankhula Mawu osalephera. Ndizo zonse zomwe iye adafunitsitsa. Iye AMATHA KUYANKHUL A, NDIPO MULUNGU ANKACHITITSA ICHO KUKWANILITSIDWA.

Vumbulutso la Uthenga uwu NDI mthenga wa Mulungu wadzoza chikhulupiriro chathu KUPOSA momwe zisanachitikepo mkale lonse. Izo zatisunthira ife mu magulu aakulu kwambiri. Izo zatilekanitsa ife ku chirichonse kupatula Uthenga Wake, Mawu Ake, Liwu Lake, Matepi Ake.

Ziribe kanthu kuti ndife ochepa bwanji, timasekedwa mochuluka bwanji, kunyozedwa, sizimatitekesa mpang’ono pomwe. IFE TIMACHIONA ICHO. IFE TIMAKHULUPIRIRA ICHO. Pali chinachake mkati mwathu. Tinakonzedweratu kuti tidzachiwone ICHO ndipo palibe chimene chidzaatilepheretsa ife kuchikhulupirira ICHO.

Ife timakumbukira zomwe masomphenyawo ananena, “bwerera ukasunge Chakudya”. Kodi nkhokweyo inali kuti? Branham Tabernacle. Kodi pali chirichonse mu dziko, kapena kuzungulira dziko kulikonse, chimene chingafanane ndi Mauthenga amene ife tiri nawo? IWO ndi Liwu lokhalo lotsimikiziridwa ndi Mulungu Mwiniwake kuti liri PAKUTI ATERO AMBUYE. LIWU LOKHALO!

Kodi ndi kutiso kumene ife tikanati, kapena tikanafuna kupita, pamene iye anati;

Apa ndi pomwe Chakudyachi chasungidwira…

Icho chasungidwa pano
Iwo uli pa matepi. Iwo uzipita ku kutambalala konse kwa dziko pa matepi, kumene anthu mu manyumba mwawo. Matepi amenewo azikafika mmanja mwa a okonzedweratu a Mulungu. Iye akhoza kuwalondolera Mawu. Iye alondolera chirichonse ndendende basi mpaka ku ntchito yake. Ndicho chifukwa Iye ananditumiza Ine kuti ndibwerere ndidzachite izi. “Kudzachisunga Chakudyacho kuno.”

Ife Ndife Mkwatibwi wa Mawu Ake Angwiro amene wakhala ndi Chakudya Chake Chosungidwa. Palibe chifukwa chomaliranso, ife timangoyankhula Mawu ndi kupita patsogolo, pakuti ife NDIFE Mawu.

Palibe chomadela nkhawa. Palibeso chifukwa chomakhalira ndi misonkhano ya mapemphero ausiku onse kuti itiwululire kuti ife ndife ndani, Mawu avumbulutsidwa kwa ife. Timadziwa kuti ndife ndani, mofanana ndi mneneri wa Mulungu, ndipo watiuza kale amene anali kupita.

“Mmodzi aliyense wa ife! Kaya ndinu mkazi wa mnyumba, kapena ndinu m—mdzakazi wamng’ono, kapena ndinu mkazi wachikulire, kapena mwamuna wamng’ono, kapena mwamuna wachikulire, kapena chirichonse chimene inu muli, ife tikupita, mulimonse. Sipakhala mmodzi wa ife ati atsalire.” Ameni. “Mmodzi aliyense wa ife akupita, ndipo ife sitiletsa kanthu kalikonse.”

Lankhulani za kutipatsa ife CHIKHULUPILIRO chokwatulitsa!!!

Bwerani mudzajowine gawo la Mkwatibwi wa Mulungu pamene ife tikusonkhana palimodzi mozungulira Liwu lotsimikiziridwa la Mulungu, pamene Iye akuyankhula ndi kutiuza ife: Wokondedwa Wanga, Wosankhidwa Wanga, Mkwatibwi Wanga, Ukulilira Chiyani, Yankhula, ndipo pita patsogolo.

M’bale. Joseph Branham

Uthenga: 63-0714M Ukulilira Chiyani? Yankhula!

Nthawi: 12:00 PM, Nthawi yaku Jeffersonville

Malo:

Koma pali Mpingo weniweni umodzi wokha, ndipo iwe sumajowina Iwo. Iwe umabadwira mwa Iwo. Mwaona? Ndipo ngati iwe wabadwira mwa iwo, Mulungu wamoyo amagwira ntchito Iyemwini kupyolera iwe, ndi kumadzipangitsa Iyemwini kudziwika. Mwaona? Ndiko kumene Mulungu amakhala, mu Mpingo Wake. Mulungu amapita ku Tchalitchi tsiku lirilonse, amakhala moyo mu Mpingo. Iye amakhala moyo mwa inu. Inu ndinu Mpingo Wake. Inu ndinu Mpingo Wake. Inu ndinu Kachisi amene Mulungu amakhalamo. Ndinu Mpingo wa Mulungu wamoyo, inueni.

25-0824 Mgonero

Uthenga: 65-1212 Mgonero

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mawu Otsimikiziridwa Mkwatibwi Yekha,

Ndife othokoza bwanji kwa Mzimu Woyera chifukwa cha Vumbulutso loona la Mawu Ake otsimikiziridwa a lero. Ambiri amadzinenera kuti amakhulupirira M’bale Branham kuti ndi mneneri wa Mulungu amene amakwaniritsa Malemba olonjezedwa a iyemwini, koma Vumbulutso loona la Mawu ndi dongosolo la Mulungu labisika kwa iwo.

Ndi kalata yachikondi iliyonse yomwe Mkwatibwi amamva, Mulungu amatsimikizira kwa ife kuti tili mu Chifuniro Chake changwiro pomvera Njira Yake yoperekedwa ya lero, Liwu la Mulungu pa Matepi.

Ndipo ife tikuyenera kumutsatira Iye, ndiyo njira yokhayo yokhalira nawo Moyo Wamuyaya. Chotero utsogoleri wa Mulungu ndi: kutsatira Mawu otsimikiziridwa a ora mwa Mzimu Woyera.

NJIRA YOKHA yopita ku Moyo Wamuyaya ndi: Mzimu Woyera ukukutsogolerani kuti muzitsatira Mawu otsimikiziridwa. Ndani ali nawo Mawu otsimikiziridwa a lero? Kodi Mulungu anamusankha ndani kuti azitanthauzira Mawu Ake? Kodi Mulungu ananena kuti linali liwu lake la ndani lero? Kodi Mulungu Mwiniwake anati ndani anali mtsogoleri wotsimikiziridwa kuti atsogolere Mkwatibwi Wake lero? Utumiki?

Chimodzimodzi monga ine ndinanena, mphungu yaing’ono pamene iyo inamva Liwu la Mkwati, iyo inapita kwa ilo, odzozedwa, Mawu otsimikiziridwa a Mulungu a tsiku lotsirizali.
Nowa anali Mawu otsimikiziridwa a tsiku lake.
Mose anali Mawu otsimikiziridwa a tsiku lake.
Yohane anali Mawu otsimikiziridwa

Iwo akhoza kupotoza chirichonse kapena kutanthauzira kulikonse kwa Iwo akufuna, koma:
WILLIAM MARRION BRANHAM NDI MAWU OTSIMIKIZIRIDWA A MULUNGU A LERO!!

Chotero utsogoleri wa Mulungu ndi: kutsatira Mawu otsimikiziridwa a ora mwa Mzimu Woyera.

Ndipo kusewera Liwu lotsimikiziridwa la Mulungu mu mpingo wanu si chinthu chofunika kwambiri chimene Mkwatibwi angachite? Ndikofunikira kwambiri kumva liwu losiyana?

Kodi ndi gulu la amuna ndi utumiki wawo umene udzalumikizana ndi kutsogolera Mkwatibwi? Kodi Mkwatibwi adzalumikizidwa ndi zomwe utumiki ukunena? Onse akunena zosiyana, ndiye titsatire ndani?

Kodi kutanthauzira kwawo kwa Uthenga uwu ndi kumene ife tidzaweruzidwa nako? Kodi iwo ali nalo Lawi la Moto likutsimikizira utumiki wawo? Kodi ndiko kutanthauzira kwawo kwa Mawu Mtheradi wanu?

Mneneri anati Mkwatibwi adzakhala WOLUMIKIZANA. Dzifunseni nokha, ndi chiyani chiti chidzachititse uneneri uwu kuti ukwanilitsidwe kuti Ambuye abwere ndi kudzamukwatula Mkwatibwi Wake?

Ndiyeno, pamene anthu a Mulungu ayamba kusonkhananso palimodzi, pamakhala chiyanjano, pamakhala mphamvu. Mukuona? Ndipo paliponse pamene anthu a Mulungu abwera palimodzi kwathunthu, ine ndikukhulupirira chiukitsiro chidzachitika apo ndiye. Padzakhala nthawi ya mkwatulo pamene Mzimu Woyera udzayamba kuwasonkhanitsa iwo. I—iwo adzakhala apang’ono, ndithudi, koma kudzakhala kuli kusonkhana kwakukulu.

Kodi padzakhala kusonkhana kwakukulu kuzungulira utumiki wa munthu wina, kupatulapo mneneri wotsimikiziridwa wa Mulungu? Kodi lidzakhala GULU la atumiki chifukwa ena mwa awutumiki wofutukuka pasanu amanena kuti MUSAMASEWERE LIWU la Mulungu mu tchalitchi mwanu, ndi zolakwika. Kodi iwo adzatsogolera Mkwatibwi ndiye?

CHONDE NDITHANDIZENI! KODI NDI MTUMIKI UTI YEMWE NDIYENERA KUMUTSATIRA POMWE NDIKUFUNA KUKHALA WOLUMIKIDWA NAWO PA PAMSONKHANO WAWUKULU UWO.

Ena amati utumiki wofutukuka pasanu a Mabingu Asanu ndi awiri adzafikitsa Mkwatibwi ku ungwiro . Atumiki ena awutumiki wofutukuka pasanu amati masiku a utumiki wa Munthu Mmodzi atha. Atumiki ena a utumiki wofutukuka pasanu amati ife tiyenera kubwerera ku Pentekosite. Ena amati Uthenga SULI M’theradi. Ena amati ukamasewera matepi ndiwe wokhulupirira milungu. Onse amanena chinachake chosiyana, ndipo ONSE ali ndi matanthauziridwe osiyana, malingaliro osiyana, koma aliyese wa iwo amanena kuti IWO akutsogozedwa ndi Mzimu Woyera.

KODI NDI MTUMIKI WUTI WA UTUMIKI WOFUTUKUKA PASANU YEMWE NDIYENERA KUMUTSATIRA? Bola ngati ine nditsatila abusa “ANGA” awutumiki wofutukuka pasanu, ine ndidzakhala Mkwatibwi? Pali “Magulu” osiyanasiyana a atumiki wofutukuka pasanu. Atumiki 20 awa amasonkhana pamodzi ndi kuchititsa misonkhano yawo, koma 20 amatsutsana kwathunthu ndi azitumiki ena amene akukhala ndi misonkhano yosiyana…ndi misonkhano iti yomwe ine ndipite kuti ndikakhale wangwiro ndi wolumikizana…ena a iwo…onse a iwo?

Ndipo anthu amakhulupilira kuti CHISOKONEZO CHIMENECHI CHILUMIKIZITSA NDIKUMUFIKITSA KU UNGWIRO MKWATIBWI? Onse amati iwo ali Atumiki WOONA AWUTUMIKI WOFUTUKUKA PASANU WOITANIDWA NDI MULUNGU. Koma iwo sakukutsogolerani inu ku UTSOGOLERI WOONA WA MZIMU WOYERA, AKUKUKUTSOGOLERANI INU KWA IWO ENI NDIKU UTUMIKI WAWO.

Kwa ine, simukusowa ngakhale vumbulutso kuti mudziwe zomwe sizingagwirizane kapena kutsogolera Mkwatibwi yense. MAWU OKHA ati adzayanjanitse Mkwatibwi, mwa LIWU LA MULUNGU YEKHA PA MATEPI.

Abale ndi alongo, kulibwino kuti mudzuke ngati mukutsatira m’busa amene akungolalikira ndi kubwereza mawu Mawu, omwe ali odabwitsa ndipo ALI NDENDENDE chimene ayenera kuchita, koma osakuuzani, ndipo chofunika kwambiri, KUCHITA, posewera LIWU LA MULUNGU PA MATEPI MU MPINGO WANU.

M’bale Branham anatiuza kuti:

Tsopano, ife tiri ndi madongosolo Auzimu atatu okha omwe atsalira kwa ife: amodzi a iwo ndi—ndi mgonero, kutsukana-mapazi, ubatizo wa madzi. Ndi zinthu zitatu zokhazo. Ndiwo ungwiro, wa zitatuzo, mwaona.

Ine ndikufuna kuti ife tikhale ndi Chiyanjano cha Mgonero ndi kutsukana Mapazi Lamlungu lino, ngati Ambuye alola. Monga tinachitirapo m’mbuyomu, ndikukulimbikitsani inu kuti muyambe nthawi ya 5:00 PM. Mu nthawi ya m’dera lanu . Ngakhale kuti M’bale Branham ananena kuti atumwi amadya Mgonero nthawi iliyonse imene iwo ankasonkhana, iye ankakonda kuti azidya iwo nthawi yamadzulo, ndipo ankawutchula kuti Mgonero wa Ambuye.

Utumiki wa Uthenga ndi Mgonero udzakhala pa Wailesi ya Liwu, ndipo padzakhalanso ulalo wa fayilo yomwe mungatsitse, kwa iwo omwe sangathe kupeza Wilesi ya Liwu Lamlungu madzulo.

M’bale Joseph Branham

25-0810 Zochitika Zamakono Zimamveka Bwino Ndi Uneneri

Uthenga: 65-1206 Zochitika Zamakono Zimamveka Bwino Ndi Uneneri

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mkwatibwi Woona ndi Wamoyo,

Pamene Yesu, Mawu Iwoeni, anabwera ku dziko lapansi zaka 2000 zapitazo, Iye anabwera monga Iye ananenera kuti Iye akanadzabwera, monga Mneneri. Mawu Ake amalengeza, kuti Iye asanabwere kachiwiri, mawonetseredwe athunthu a Umunthu wa Yesu Khristu adzawonetseredwa kachiwiri mu thupi, mwa mneneri. Mneneri ameneyo wabwera, dzina lake ndi William Marrion Branham.

Kodi wina aliyense angalephere bwanji kuzindikira kuti kumvera Liwu la Mulungu kumalankhula ndi iwo mwachindunji pa matepi kuti ndicho Chifuniro changwiro cha Mulungu? Ife tikudziwa kuti Mawu nthawizonse amadza kwa mneneri Wake; Sizingabwere mwanjira ina iliyonse. Izo ziyenera kubwera kupyolera mu njira ya Mulungu imene Iye anatiwuziratu kale za iyo . Ndi njira yokhayo yomwe Izo zidzadzere konse. Mulungu amayenda mu njira imene Iye analonjeza kuti Iye akanadzachita izo. Iye samalephera konse kuchita izo mwanjira yomweyo yofanana momwe Iye nthawizonse ankachitira.

Wina aliyense wa iwo ankadya chinthu chomwecho, iwo onse ankavina mu Mzimu, iwo onse anali nacho chirichonse mofanana; koma pamene izo zinafika ku nthawi yolekanitsidwa, Mawu ndi omwe analekanitsa. Mmomwe izo zirili lero! Mawu ndi omwe amalekanitsa! Pamene ifika nthawi yake,

Ife tikuwona kuti nthawi ikuchitika tsopano, Mawu akulekanitsa. Mkwatibwi akuimbidwa mlandu wa kuyika zochuluka kwambiri pa mneneri pamene iwo amati, “Pali amuna ena oyitanidwa ndi Mulungu, odzazidwa ndi Mzimu Woyera kuti atsogolere Mkwatibwi lero.” Inu mukusowa zochuluka kuposa matepi okha.Mulungu wayika amuna lero kuti atsogolere mpingo

“Iwe ukuyesera kumaganiza kuti ndiwe mmodzi wekha bwinoko kuposa izo. Ndipo iye anati, “Chabwino, gulu lonseli ndi loyera. Iwe ukuyesera kumadzipanga wekha…” Ngati ife tikanati tinene izo lero, kayankhulidwe ka pa msewu, “Nsangalabwi yokha ya pa doko.”

Ndipo Mose ankadziwa kuti Mulungu anali atamutuma iye uko chifukwa cha izo.

Mulungu ali nawo amuna odzazidwa ndi Mzimu Woyera kuti azitsogolera Mkwatibwi Wake; kuwatsogolera iwo KU PAKUTI ATERO AMBUYE, MNENERI MTHENGA. Pakuti Uthenga ndi m’thenga ali wofanana. Imeneyo ndiyo njira ya Mulungu yosasintha yoperekedwa ya tsiku la lero, ndiponso nthawi zonse.

Chifukwa iwo anamvetsera kwa cholakwika. Pamene Mose, wotsimikizidwira ndi Mulungu, ndi mtsogoleri kuti awasonyeze iwo njira yaku Dziko Lolonjezedwa, ndipo iwo anali atabwera patali chotere bwinobwino, komano iwo sakanakhoza kupitirira limodzi naye.
Tsopano, okhulupirira akhoza kuwaona Iwo, koma osakhulupirira sangakhoze kuwawona Iwo akutsimikizidwira.

Osati kokha kuti inu munasankhidwa kuti mulandire Vumbulutso lalikulu la nthawi yotsiriza ili la lero, koma Mulungu, mwa njira ya matepi Ake a Chakudya chosungidwa, amalankhula pakati pa mizere kwa Mkwatibwi Wake wokoma wa pamtima.

Ndiye ngati inu muli mwana wamwamuna wa Mulungu kapena mwana wamkazi wa Mulungu, inu munali mwa Mulungu nthawiyonseyo. Koma Iye ankadziwa kama wake ndi nthawi yomwe inu mukanati mudzabzalidwe. Kotero tsopano inu mwapangidwa cholengedwa, mwana wamwamuna wa Mulungu, mwana wamwamuna kapena wamkazi wa Mulungu wowonetseredwa kuti mukomane ndi chitsutso cha ora lino kuti mutsimikizitsire Mulungu woona ndi wamoyo wa ora lino, Uthenga umene ukubwerapowu mu nthawi ino. Uko nkulondola! Inu munapangidwa uko asanakhazikitsidwe maziko a dziko.

Ndi kalata yachikondi bwanji yapakati pa mizere kwa Mkwatibwi Wake, ULEMERERO!!! Osati kokha kuti Iye anatidziwa ndi kutisankha ife asanaikidwe maziko a dziko, koma pano Iye akutiuza ife kuti Iye anatisankha ife kuti tikhale ana Ake aamuna ndi aakazi owonetseredwa a LERO. Iye anatiika ife pano pa dziko lapansi lero, pamwamba pa oyera mtima ena onse kuyambira pachiyambi, chifukwa Iye ankadziwa kuti ife tikanati tidzakumane ndi vuto la ora lino kuti titsimikizire Mulungu woona ndi wamoyo wa ora lino, Uthenga umene ukubwera mu nthawi ino.

Ife tinali mwa Mulungu, jini, mawu, chikhumbo kuchokera kuchiyambi, koma TSOPANO Ife tikukhala PAMODZI mu malo Ammwambamwamba mwa Khristu Yesu, kuyankhulana ndi Iye mwa Mawu Ake, kupyolera mu Mawu Ake; pakuti ife NDIFE MAWU AKE, ndipo Iwo akudyetsa miyoyo yathu.

Sitingathe, ndipo sitidzabayilamo kalikonse m’miyoyo yathu koma Mawu osaipitsidwa a Mulungu. Timazindikira ndikukhulupirira kuti ndi njira yoperekedwa ndi Mulungu ya lero.

Ife tikanakonda kuti inu mubwere kuzajowinana nafe Lamlungu lino pa 12:00 p.m., nthawi ya ku Jeffersonville, pamene ife tikumva LIWU LOKHA, Liwu la Mulungu pa matepi, inu mukhoza kunena kuti AMEN kwa Mawu aliwonse omwe inu mumawamva.

M’bale. Joseph Branham

Uthenga: Zochitika Zamakono Zimamveka Bwino Ndi Uneneri 65-1206

Malemba oti muwerenge musanamve Uthenga:

Genesis 22
Deuteronomo 18:15
Masalimo 16:10 / 22:1 / 22:18 / 22:7-8 / 35:11
Yesaya 7:14 / 9:6 / 35:7 / 50:6 / 53:9 / 53:12 / 40:3
Amosi 3:7
Zekariya 11:12; 13:7/14:7
Malaki 3:1/4:5-6
Mateyu woyera 4:4 / 24:24 / 11:1-19
Luka woyera 17:22-30 / 24:13–27
Ahebri 13:8; 1:1
Yohane Woyera 1:1
Chivumbulutso 3:14-21; 10:7

25-0803 Zinthu Zimene Ziti Zidzakakhaleko

Uthenga: 65-1205 Zinthu Zimene Ziti Zidzakakhaleko

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Zikhumbo za Mulungu,

Mawu aliwonse amene analankhulidwa mu Uthenga uwu ndi kalata yachikondi kwa Mkwatibwi Wake. Kuganiza kuti Atate wathu wa Kumwamba amatikonda kwambiri, moti sikuti ankangofuna kuti tiziwerenga Mawu ake, koma ankafuna kuti tizimva Liwu lake likulankhula ku mitima yathu kuti atiuze kuti: “Inu ndinu liwu langa lamoyo, Chikhumbo changa chamoyo, chimene Ine ndingawonetsere pa dziko lapansi.

Ndiyeno kuganiza kuti pambuyo pa nsembe Yake yonse imene Iye anachita pano pa dziko lapansi, moyo umene Iye anakhala, njira imene Iye anayenda. Iye anapempha chinthu chimodzi,

“Kuti kumene Ine ndikakhale, iwonso akakhaleko.” Iye anapempha chiyanjano chathu. Ndicho chinthu chokhacho chimene Iye anawapempha Atate mu pemphero, ubwenzi wanu wosatha.

Kumene ine ndiri, “Mawu Ake,” ifeso tiyenera kukakhalako, kuti tikalandire chiyanjano Chake, Ubwezi Wake Wosatha, kwanthawizonse. Chotero, tiyenera kukhala moyo mwa Mawu aliwonse amene Iye analankhula kwa ife pa matepi kuti tikhale Namwali m’kwatibwi wa mawu, amene amatipanga ife gawo la Mkwati.

Ilo ndilo VUMBULUTSO la Yesu Khristu mu ora lino. Osati chimene Iye anali mu ora lina, yemwe Iye ali TSOPANO. Mawu a lero. Kumene Mulungu ali lero. Ndilo Vumbulutso la lero. Tsopano likukula mwa Mkwatibwi, kutipanga ife mu m’thunthu lokwana la mngwiro la ana aamuna ndi aakazi.

Ife timadziwona tokha mu Mawu Ake. Ife tikudziwa amene ife tili. Ife tikudziwa ife tiri mu dongosolo Lake. Iyi ndi Njira yoperekedwa ndi Mulungu ya lero. Ife tikudziwa Mkwatulo uli pafupi. Posachedwapa okondedwa athu adzawonekera. Kenako tidzadziwa: kuti Ife Tafika. Ife tonse tikupita Kumwamba…inde, Kumwamba, malo enieni monga awa.

Ife tikupita kumalo enieni kumene tizikachitako zinthu, kumene tikakhalako moyo. Ife tizikagwirako ntchito. Ife tikasangalalako. Ife tikakhalako moyo. Ife tikupita ku Moyo, ku Moyo Wamuyaya weniweni. Ife tikupita Kumwamba, paradiso. Chimodzimodzi monga momwe Adamu ndi Eva ankagwirira ntchito, ndi kumakhala moyo, ndi kumadya, ndi kumasangalalako, mmunda wa Edeni tchimo lisanabweremo, ife tiri panjira yathu tikubwerera kumeneko panonso, kulondola, tikubwerera kumeneko. Adamu woyamba, chifukwa cha tchimo, anatichotsako ife. Adamu Wachiwiri, kupyolera mu chirungamo, akutibwezeretsako ife kumeneko kachiwiri; akutilungamitsa ife ndi kutibwezeretsanso ife mmenemo.

Kodi aliyense anganene bwanji za izi pazomwe izo zikutanthauza kwa ife? Chowonadi ndi chakuti tikupita ku paradaiso kumene tikukakhala kwa Muyaya wonse pamodzi. Kulibenso chisoni, zowawa kapena Zokhumudwitsa, ungwiro basi pa ungwiro.

Mitima yathu ikukondwera, miyoyo yathu ili pamoto mkati mwathu. Satana akumayika mochuruka ndi mochuruka zopsinja pa ife tsiku lililonse , koma ife tikusangalalabe. Chifukwa:

  • TIKUDZIWA, YEMWE IFE TILI.
  • TIKUDZIWA, SITINAMULEPHERE, NDIPO SITIDZAMULEPHERA IYE.
  • TIKUDZIWA, TILI MU CHIFUNIRO CHAKE CHANGWIRO.
  • TIKUDZIWA, WATIPATSA IFE VUMBULUTSO LOWONA LA MAWU AKE.

M’bale Joseph, inu mumalemba chinthu chomwecho sabata iliyonse. ULEMERERO, ndidzalemba chimenecho sabata iliyonse chifukwa Iye akufuna kuti inu mudziwe mochuruka momwe Iye amakukonderani inu.Yemwe inu muli. Kumene inu mukupita. Chithunzi chikusandulika kukhala chenicheni. Inu ndinu Mawu mukusandulika kukhala Mawu.

Okondedwa dziko, bwerani mudzajowinane nafe Lamlungu lino pa 12:00 p.m., nthawi ya ku Jeffersonville, polumikizana, osati chifukwa “Ine” ndikukuitanani inu, koma chifukwa “IYE” akukuitanani inu. Osati chifukwa “Ine” ndinatenga tepiyo, koma kumva Mawu ndi gawo la Mkwatibwi kuzungulira dziko lonse nthawi imodzi.

Kodi Ife tingazindikire kuti n’zotheka kuti Mkwatibwi amve Liwu la Mulungu padziko lonse, pa nthawi yofanana? Ameneyo ayenera kukhala Mulungu. Mulungu anali ndi mneneri wake kuti achite izo pamene mngelo Wake anali pano pa dziko lapansi. Iye analimbikitsa Mkwatibwi kulumikizana mu m’pemphero, ONSE PA NTHAWI YOFANANA YA KU JEFFERSONVILLE, 9:00, 12;00, 3:00; Kodi icho ndi chinthu chachikulu motani tsopano, kuti Mkwatibwi akhoza kulumikizana ngati M’MODZI kuti amve Liwu la Mulungu likuyankhula kwa iwo onse pa nthawi imodzi?

M’bale. Joseph Branham

Uthenga: Zinthu Zimene Ziti Zidzakakhaleko 65-1205

Malemba:
Mateyu woyera 22:1-14
Yohane Woyera 14:1-7
Ahebri 7:1-10

25-0727 Mkwatulo

Uthenga: 65-1204 Mkwatulo

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mkwatibwi Wopanda mangawa,
 
 
Ambuye anatipatsa ife nthawi yodabwitsa kwambiri pa msasa sabata yatha pamene Iye anatiululira Mau ake kwa ife. Iye anatsimikizira, mwa Mawu Ake, kuti Mtheradi wathu uli: Mawu Ake, Uthenga uwu, Liwu la Mulungu pa matepi; onse ali ofanana, Yesu Kristu yemweyo dzulo, lero, ndi kunthawi zonse. 
 
Tinamva mmene mdierekezi amayesera kulekanitsa Uthenga kwa mthengayo, koma Ambuye Yesu alemekezeke, Mulungu mwini analankhula kudzera mwa mngelo wake wamphamvu natiuza kuti:

Ife tikupeza apo kuti pamene munthu abwera, atatumidwa kuchokera kwa Mulungu, wodzozedwa ndi Mulungu, ndi PAKUTI ATERO AMBUYE woona, uthenga ndi mtumiki ali mmodzi ndi ofanana. Chifukwa iye watumidwa kuti adzayimire PAKUTI ATERO AMBUYE, Mawu ndi Mawu, kotero iye ndi uthenga wake ali ofanana.

Inu simungakhoze kulekanitsa Uthenga kwa mtumikiyo, iwo ali ofanana, PAKUTI ATERO AMBUYE. Ziribe kanthu zomwe wodzozedwa wabodza aliyense akunena, Mulungu anati iwo ali ofanana ndipo sangalekanitsidwe.
 
Ndiye Iye anatiuza ife kuti sitikusowa chiguduli chosefera kuti tigwire zipumbu zonse pomwe ife tikumvetsera ku matepi, pakuti mulibe nsikidzi kapena madzi a sikidzi mu Uthenga uwu. Ndi chitsime Chake cha kasupe chomwe chimayenda madzi nthawi zonse oyera ndi awukhondo. Nthawizonse akutumphukabe pamwamba, sichimawuma ayi, kumangopitirira kukankhira ndi kukankha, kumatipatsa ife Vumbulutso lochulukira la Mawu Ake.
 
Anatikumbutsa kuti tisaiwale kuti pangano lake ndi ife ndi Losatsutsika, Losatsutsika, koma koposa zonse, Lopanda mangawa.
 
Kaya ndi chikondi, chithandizo, kapena kugonja, ngati china chake chopanda mangawa ndi MTHERADI ndipo sichigwirizana ndi mfundo kapena zikhalidwe zina zapadera: izo zichitika zivute zitani.
 
 Ndiye Iye anafuna kukhomerera msomali, kotero anatiuza ife kuti lero Malemba Ake akukwaniritsidwa pamaso pathu.

Kuti d-z-u-w-a lomwelo limene limatuluka kummawa ndi d-z-u-w-a lomwelo limene limadzalowa kumadzulo. Ndipo M-w-a-n-a wa Mulungu yemweyo amene anabwera kummawa ndi kudzadzitsimikizira Yekha ngati Mulungu wowonetseredwa mu thupi, ndi M-w-a-n-a wa Mulungu yemweyo kumadzulo kwa dziko lapansi kuno, amene akudzizindikiritsa Yekha pakati pa mpingo usikuuno, yemweyo dzulo, lero, ndi kwanthawizonse. Kuwala kwa kumadzulo kwa Mwana kwafika. Lero Lemba ili lakwaniritsidwa pamaso pathu.

 Mwana wa Munthu wabweranso mu thupi laumunthu mu tsiku lathu, monga momwe Iye analonjezera kuti Iye akanadzatero, kuti adzaitane Mkwatibwi. Ndi Yesu Khristu akuyankhula molunjika kwa ife, ndipo Izo sizikusowa kutanthauzira kwa munthu. Zonse zomwe tikusowa, zomwe tikufuna, ndi Liwu la Mulungu loyankhula pa tepi lochokera kwa Mulungu Mwiniwake.

Ndi vumbulutso la kukwaniritsika kwa Mawu kukhalitsidwa owona. Ndipo ife tikukhala mu tsiku limenelo. Mulungu alemekezeke! Vumbulutso la chinsinsi la Iyemwini.

Ndi nthawi yaulemerero bwanji yomwe Mkwatibwi ali nayo, ali mu kukhalapo kwa Mwana, akucha. Tirigu wabwereranso ku tirigu, ndipo palibe chotupitsa pakati pathu. Liwu loyera la Mulungu loyankhula kwa ife, kutiumba ndi kutipanga ife mu chifaniziro cha Khristu, Mawu.
 
 
Ife ndife ana aamuna ndi aakazi a Mulungu, chikhumbo Chake chimene Iye anachikonzeratu kuti chibwere mu m’badwo uno, m’badwo waukulu kwambiri mu mbiriyakale ya dziko.  Iye ankadziwa kuti ife sitikanati tilephere, ife sitikanati tinyengerere, koma ife tikanakhala Mkwatibwi Wake wa Mawu owona ndi wokhulupirika, Mbewu Yake Yachifumu yolonjezedwa Yapamwamba ya Abrahamu yomwe inali nkudza.
 
Mkwatulo uli pafupi. Nthawi yafika kumapeto. Iye akudzera Mkwatibwi Wake yemwe wadzikonzekeretsa Yekha koma akukhala mu Kukhalapo kwa Mwana, akumva Liwu Lake kumuveka Mkwatibwi Wake. Posachedwapa tidzayamba kuona okondedwa athu omwe ali kuseri kwa ketani ya nthawi, omwe akuyembekezera ndi kulakalaka kukhala nafe.

Matepi ndi njira yoperekedwa ndi Mulungu kuti afikitse Mkwatibwi Wake ku ungwiro. Matepi awa ali chinthu chokha chimene chidzagwirizanitsa Mkwatibwi Wake. Matepi awa ali Liwu la Mulungu kwa Mkwatibwi Wake.
 
Ine ndikukuitanani inu kuti mubwere ndi kudzalumikizana nafe, gawo la Mkwatibwi Wake, Lamlungu lino pa 12:00 p.m., nthawi ya ku Jeffersonville, pamene ife tikumva zonse za zomwe zikukonzekera kuti zichitike posachedwapa: Mkwatulo 65-1204. 

 
M’bale. Joseph Branham

25-0720 Pa Mapiko A Nkhunda Yoyera-mwachipale

Uthenga: 65-1128E Pa Mapiko A Nkhunda Yoyera-mwachipale

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mkwatibwi wa Khristu, tiyeni ife tibwere palimodzi Lamlungu 12:00 P.M., nthawi ya ku Jeffersonville, kuti tidzamve 65-1128E Pa Mapiko A Nkhunda Yoyera-mwachipale
M’bale. Joseph Branham

25-0713 Malo Okhawo Operekedwa Ndi Mulungu Opembedzerapo

Uthenga: 65-1128M Malo Okhawo Operekedwa Ndi Mulungu Opembedzerapo

PDF

BranhamTabernacle.org

Lokondedwa Banja la Yesu Khristu,

Chinachake chikuchitika kuposa kale ndi Mkwatibwi wa Khristu padziko lonse lapansi. Zinthu zomwe tazimva ndi kulakalaka kuziwona tsopano zikuwonetseredwa pamaso pathu.

Mzimu Woyera ukugwirizanitsa Mkwatibwi Wake monga Iye anati Iye akanadzatero, mwa njira Yake YOKHA yoperekedwa ya lero, Liwu la Mulungu pa matepi.

Iye akuwulula ndi kutsimikizira Mawu Ake kuposa kale. Mofanana ndi chitsime cha kasupe, Chibvumbulutso chikutumphuka mkati mwathu.

Chilumikizano chauzimu chija cha Khristu ndi Mpingo Wake tsopano, pamene mnofu ukusandulika Mawu, ndipo Mawu akusandulika mnofu, kuwonetseredwa, kutsimikiziridwa. Basi zomwe Baibulo linati zikanadzachitika mu tsiku lino, izo zikuchitika, tsiku ndi tsiku. Bwanji, izo zikuwunjikana mofulumira kwambiri kunja uko, mu zipululu izo, ndi zinthu zomwe zikuchitika, mokuti ine sindingakhoze ngakhale kuyendera limodzi nazo izo.

Tsiku ndi tsiku Chivumbulutso chochuluka chikuwululidwa ndikuwonetseredwa kwa ife. Monga mneneri, zinthu zikuchitika ndipo zikuchitika mofulumira kwambiri, sitingathe ngakhale kupitiriza nazo … ULEMERERO!!!

Nthawi yathu yafika. Lemba likukwaniritsidwa. Thupi likukhala Mawu, ndipo Mawu akukhala thupi. Basi zomwe mneneri ananena kuti zikanadzachitika tsopano zikuchitika.

Kodi ndi Chifukwa chiyani ife?

Palibe chotupitsa, kapena mawu osadziwika, palibe kutanthauzira kwa munthu kofunika pakati pathu. Timangomvetsera Mawu Oyera Angwiro kuchokera mkamwa mwa Mulungu pamene Iye akulankhula kwa ife milomo ndi khutu.

Tsopano ife tikuwaona Mawu olonjezedwa omwewo, a Luka, a Malaki, malonjezo onse awa kuyambira lero, akupangidwa thupi, akukhala pakati pa ife, amene ife tinawamva ndi makutu athu; tsopano ife tikumuwona Iye (ndi maso athu) akutanthauzira Mawu Ake Omwe, ife sitikusowa kutanthauzira kulikonse kwa munthu.

Mkwatibwi, izo mophweka sizikanakhoza kumveka bwino kuposa izo. Iye ndi Mulungu, atayima pamaso pa Mkwatibwi Wake mu thupi laumunthu, yemwe ife tikhoza kumuwona ndi maso athu omwe, akuyankhula ndi kutanthauzira Mawu Ake Omwe, ndi kuwayika iwo pa tepi. Mawu Angwiro olankhulidwa ndi kulembedwa ndi Mulungu Mwiniwake, motero samasowa kutanthauzira kulikonse kwa munthu.

  • Mulungu akuyankhula molunjika kwa Mkwatibwi Wake, pa matepi.
  • Mulungu akutanthauzira Mawu Ake Omwe, pa matepi.
  • Mulungu akudziwulula Yekha, pa matepi.
  • Mulungu akumuuza Mkwatibwi Wake, inu simukusowa kutanthauzira kulikonse kwa munthu, Mawu Anga pa matepi ali zonse ZOFUNIKIRA MKWATIBWI WANGA.

Kumbukirani, pamene inu muchoka pano, muyambe kuchokamo mu mankhusu tsopano; inu mukupita mu njere, koma mukakhale mu Kukhalapo kwa Mwana. Musakawonjezere, zimene ine ndanena; musakachotsere, zimene ine ndanena. Chifukwa, ine ndimayankhula Choonadi monga momwe ine ndikudziwira Icho, monga Atate andipatsira ine. Mukuona?

Mulungu wapanga NJIRA YABWINO YOKHAYO kuti Mkwatibwi achite monga momwe anatilamulira ife. Izi sizinachitikepo, mpaka lero. Palibe kungoganiza, popanda kudabwa, palibe funso ngati pali china chowonjezera, chochotsedwa, kapena kutanthauzira. Mkwatibwi wapatsidwa Chibvumbulutso chenicheni: KUSEWERA MATEPI NDI NJIRA YABWINO YA MULUNGU.

Ngati zingachitike, ndiroleni ndinenenso. Vumbulutso langa liri kuti Mkwatibwi wa Yesu Khristu, osati ena, MKWATIBWI, sasowa CHINTHU CHINA CHILICHONSE AYI koma Liwu la Mulungu pa matepi.

Koma pamene Mzimu Woyera uwo kwenikweni Mawu enieni abwera mwa inu (Mawu, Yesu), ndiye, m’bale, Uthenga si chinsinsi kwa inu kenako; inu mukuchidziwa Icho, m’bale, Icho chonse chawala pamaso panu.

Uthenga si chinsinsi kwa ine. Yesu Khristu ali yemweyo dzulo, lero, ndi kunthawi zonse. Kumwamba ndi dziko lonse lapansi zimatchedwa Yesu. Yesu ndiye Mawu.

Ndipo Dzinalo liri mu Mawu chifukwa Iye ali Mawu. Ameni! Iye ndi chiyani ndiye? Mawu otanthauziridwa ndi mawonetseredwe a Dzina la Mulungu.

Mulungu akulumikiza Mkwatibwi Wake ndi Liwu Lake, limene Iye analilemba ndi kulisungira kwa lero, kotero kuti Iye akhoze kubweretsa Mkwatibwi Wake palimodzi ngati Chigawo Chimodzi. Mkwatibwi aziwona izo ndi kuzizindikira Iyo ngati NJIRA YOKHAYO yomwe Iye angakhoze kubweretsa Mkwatibwi Wake palimodzi.

Iye anachita zimenezi zaka zoposa 60 zapitazo kuti atisonyeze mmene angachitire zimenezi masiku ano. Ndife “m’modzi mwa mipingo yake yomwe ikugwirizana”

Ngati ine sindikhulupirira mu kupita kutchalitchi, nchifukwa chiyani ine ndiri ndi tchalitchi? Ife tinali nawo iwo onse kudutsa m’dzikoli, titalumikizitsana usiku wina, mailosi thuu handiredi aliwonse a mabwalo anali ndi imodzi ya matchalitchi anga.

Atumiki ambiri amauza mipingo yawo kukhala pa “kulumikizana” kapena “kukhamukira”, “kumvera Uthenga womwewo nthawi imodzi”, sikupita kutchalitchi. IYE ANANGOTI IZO ZINALI! Iwo mwina sakudziwa Mawu kapena sangathe kuwerenga kalata yachikondi monga Mkwatibwi angachitire.

Kodi mpingo ndi chiyani? Tiyeni tingowona zomwe M’bale Branham ananena kuti zinali mpingo.

Magulu ambirimbiri, ali nawo malo awa omwe inu nonse munali nawo kuno kuchokera ku kachisi. Izo zalumikizidwanso ku Phoenix, kuti kulikonse kuli msonkhano, izo zikufika kumene umo…Ndipo iwo akusonkhana mu matchalitchi ndi mmanyumba, ndi zinthu monga choncho, zikudutsa mu mpweya wa mawu wabwino kwambiri.

M’bale Branham akunena momveka bwino kuti anthu mu “nyumba” zawo ndi “zinthu zonga izo” inali imodzi mwa mipingo yake yomwe inali yolumikizana. Motero nyumba, malo opangira mafuta, nyumba, mabanja osonkhanitsidwa pamodzi pa hook up ake anapanga mpingo.

Tiyeni tiwerenge KALATA YA CHIKONDI mwakanthawi kochurukilapo pang’ono

Ife tikupempherera mipingo yonse ndi magulu amene asonkhana pozungulira zo—zo—zoyankhulira zazing’ono kunja kudutsa, kuchokera ku fukoli, njira yonse mpaka ku Gombe la Kumadzulo, kukwera mpaka ku mapiri a Arizona, kutsika mpaka ku zigwa za Texas, njira yonse mpaka ku Gombe la Kummawa, monse kudutsa dziko, Ambuye, kumene iwo asonkhana. Maora ambiri motalikana, ife tiri mu nthawi, koma, Ambuye, ife tiri limodzi usikuuno ngati chimango chimodzi, okhulupirira, tikuyembekezera Kudza kwa Mesiya.

Kotero kukhala pa Kulumikizana, kumvetsera kwa M’bale Branham ONSE PA NTHAWI YOFANANA; iwo anali pamodzi ngati gulu limodzi, okhulupirira, kuyembekezera Kudza kwa Mesiya.

Koma mukunena kuti ngati muchita izi lero, kuti uko sindiko kupita kutchalitchi, izo ndizolakwika, sikumasonkhana pamodzi monga momwe tikuwonera tsiku likuyandikira, sikupita kutchalitchi kodi?

Ndiroleni ine ndikufunseni inu funso ndipo inu muwayankhe osonkhana anu. Ngati M’bale Branham akanakhala pano lero, mu thupi, ndipo inu mukanakhoza kukhamukira kapena kulumikizana kuti mumumve iye Lamlungu lirilonse mmawa, Onse pa nthawi imodzi ndi Mkwatibwi kuzungulira dziko, azibusa, kodi inu mungagwirizane ndi kumumva M’bale Branham kapena kodi inu mungalalikire?

M’bale Branham momveka akunena kuti ntchito yanu ndi mpingo wanu. Ngati inu munali kuno zaka makumi asanu ndi chimodzi zapitazo ndipo M’bale Branham anali ndi utumiki, koma mpingo wanu sunapiteko koma kukhala ndi utumiki wawo (umene atumiki ambiri ankachitira kalelo), kodi inu mungapite ku “mpingo wanu”, kapena kodi inu mungapite ku “Branham Tabernacle” kuti mukamve M’bale Branham?

Ndikupatsani yankho langa. Ine ndikanakhala nditaima pakhomo mu mvula, matalala kapena mphepo yamkuntho kuti ndilowe mu Kachisi kuti ndimve mneneri wa Mulungu. Ngati ndikanapita ku mpingo wina uja, ndikanasintha matchalitchi usiku womwewo.

Koma mkazi ameneyo, iye sankadziwa ngati mphamvu inali mu ndodo kapena ayi, koma iye ankadziwa kuti Mulungu anali mwa Eliya. Ndiko kumene Mulungu anali: mwa mneneri Wake. Iye anati, “Monga Ambuye ali wa moyo, ndiye kuti solo yanuso ili moyo, ine sindidzakusiyani inu.”

Ine ndikukuitanani inu kuti mutijowine ife ndi kukhala mmodzi wa mipingo ya M’bale Branham pa nthawi yolumikizirana Lamlungu 12:00 P.M., nthawi ya ku Jeffersonville, pamene ife tikumva Liwu la Mulungu likutibweretsera ife Uthenga: Malo Okhawo Operekedwa Ndi Mulungu Opembedzerapo 65-1128M.

M’bale. Joseph Branham

25-0706 Ine Ndakhala Ndikumva Koma Tsopano Ine Ndawona

Uthenga: 65-1127E Ine Ndakhala Ndikumva Koma Tsopano Ine Ndawona

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mkwatibwi Wolumikizidwa,

Lero, Mawu awa amene Mulungu analankhula kupyolera mwa Mngelo Wake Wachisanu ndi chiwiri akukwaniritsidwabe kupyolera mwa IFE, MKWATIBWI WA YESU KHRISTU.

Ngati ine sindikhulupirira mu kupita kutchalitchi, nchifukwa chiyani ine ndiri ndi tchalitchi? Ife tinali nawo iwo onse kudutsa m’dzikoli, titalumikizitsana usiku wina, mailosi thuu handiredi aliwonse a mabwalo anali ndi imodzi ya matchalitchi anga.

Iwo anali m’matchalitchi, m’nyumba, m’nyumba zing’onozing’ono, ndipo ngakhale pokwerera mafuta; anamwazikana kudutsa United States, akumvetsera, zonse pa nthawi imodzi yomweyo pomwe Mawu anali kupita.

Ndipo lero, ife tikadali MMODZI WA MIPINGO YAKE. Iye akadali M’BUSA WATHU. Mawu Ake SAMASOWABE KUTANTHAUZIDWA, ndipo ife tikanali osonkhanitsidwa pa dziko lonse, WOl pa MODZI, kumvetsera ku LIWU la Mulungu kumupanga kukhala wa gwiro Mkwatibwi wa Yesu Khristu.

Lero, Mawu awa akukwaniritsidwabe.

N’cifukwa ciani anali kucita zimenezo kalelo? Chifukwa chiyani abusa anatseka mipingo yawo kuti asamvere Uthenga nthawi yomweyo? Iwo akanangoyembekezera kuti atenge matepi, ndiyeno nkumalalikira Uthenga iwoeni kwa anthu awo kenako; ndipo ndikutsimikiza kuti ambiri opanda bvumbulutso Ankachita izi.

Kapena mwinamwake ena adawuza mipingo yawo, “Tsopano mvetserani, ife timakhulupirira M’bale Branham kuti ndi mneneri wa Mulungu, koma iye sananene kuti ife timayenera kumamvetsera kwa iye mu mipingo yathu. Ine ndikulalikira Lamlungu lino, ndi Lamlungu lirilonse;

Kenako Mkwatibwi , monga Mkwatibwi chabe tsopano, anali ndi Vumbulutso, ndipo ankafuna kumva Liwu la Mulungu mwachinjunji kwa iwo eni. Iwo ankafuna kuti akhale olumikizana ndi Mkwatibwi kuzungulira dziko kuti amve Liwu la Mulungu pamene ilo linali kunveka. Iwo ankafuna kuti azindikiritsidwe ngati umodzi wa mipingo yake, nyumba, kapena kulikonse kumene iwo anali, ndi Uthenga, Liwu, ndipo tsopano matepi.

Lero, Mawu awa akukwaniritsidwabe.

Chifukwa chiyani iwo/ife tinachiwona Icho ndipo ena sanachiwone? Mwa kudziwiratu, ife tinadzozedweratu kuti tiziwone Izi. Koma inu amene simunadzozedwe, simudzaziwona konse Izo. Tirigu akuwawona Iwo ndipo wayamba kuchokapo.

Izi sizikutanthauza kuti muyenera kusiya kupita kutchalitchi chanu. Komanso sizikutanthauza kuti abusa anu asiye kutumikira. Mophweka izi Zikutanthauza kuti mautumiki ambiri ndi azibusa aiwala CHINTHU CHENICHENI, ndiko kusawawuza anthu awo kuti MAWU OFUNIKA KWAMBIRI omwe muyenera kuwamva ndi LIWU la Mulungu pa matepi.

Kupita ku tchalitchi tsiku lililonse sabata iliyonse sikukupanga iwe kukhala Mkwatibwi; chimenecho sichofunikira cha Mulungu. Afarisi ndi Asaduki anali ndi chiphunzitso chimenecho kumusi uko. Iwo ankadziwa chilembo chirichonse cha Mawu aliwonse, koma Mawu Amoyo anali ataima POMWEPO mu thupi la munthu, koma kodi iwo anachita chiyani? Chinthu chomwecho chimene ambiri amachita lerolino.

Iwo amati, “Izo zinali zipembedzo zimene iye anali kuzikamba.” Iwo samamulola M’bale Branham mu mipingo yawo kuti azilalikira, koma ife timalalikira Mawu ndi kunena mobwereza basi zomwe iye ananena.

Izi ndizodabwitsa. Ambuye alemekezeke. Ndi zomwe muyenera kuchita. Koma Kenako mkumati, lero ndi zosiyana, ndi zolakwika kumasewera matepi a M’bale Branham mu tchalitchi chanu. Inu apo simuli osiyana ndi Afarisi ndi Asaduki, kapena zipembedzo.

Ndiwe wa chinyengo.

Monga zinaliri pamenepo, Ndi Yesu, atayima pakhomo akugogoda, kuyesera kuti alowe kuti ayankhule mwachinjunji kwa Mpingo Wake, ndipo iwo sadzatsegula zitseko zawo, ndipo sadzasewera matepi mu mipingo yawo. “Iye sakubwera mu mpingo wathu ndi kudzalalikira”.

Mdaniyo azipotoza izo ndikuzivunguza mbali zochuruka momwe iye AMADANA ndikuyalutsidwa, komabe, zikuwonekera pamaso pathu pomwe ndipo ambiri akuchoka.

“Pa chiyambi panali” [Osonkhana ati, “Mawu”—Mkonzi.] “ndipo Mawu anali ndi” [“Mulungu,”] “Ndipo Mawu anali” [“Mulungu.”] “Ndipo Mawu anapangidwa thupi ndipo anadzakhala pakati pathu.” Ndi kulondola uko? Tsopano ife tikuwaona Mawu olonjezedwa omwewo, a Luka, a Malaki, malonjezo onse awa kuyambira lero, akupangidwa thupi, akukhala pakati pa ife, amene ife tinawamva ndi makutu athu; tsopano ife tikumuwona Iye (ndi maso athu) akutanthauzira Mawu Ake Omwe, ife sitikusowa kutanthauzira kulikonse kwa munthu. O mpingo wa Mulungu Wamoyo! pano ndi pa lamya! dzukani mwamsanga, nthawi isanathe!

Tsegulani mitima yanu ndi kumva zimene Mulungu wanena kwa inu, mipingo yake yonse. Tsopano ife tikumuwona IYE, ndi maso athu, AKUTANTHAWUZILA MAWU AKE OMWE. Sitikufuna kutanthauzira kulikonse kwa munthu!! DZUKANI NTHAWI ISANATHE!!

Tamva za zinthu izi moyo wathu wonse zimene zikanati zidzachitike mu nthawi yotsiriza. Tsopano tikuwona ndi maso athu zikuchitika.

Iye anatiuza ife, pali NJIRA IMODZI YOKHA, IYO NDI NJIRA YOPEREKEDWA YA MULUNGU IYE ANAPANGIRA MKWATIBWI WAKE. MUYENERA KUKHALA NDI LIWU LA MULUNGU PA TEPI.

Ndikuitana dziko kuti libwere kudzalumikizana nafe Lamlungu pa 12:00 p.m., nthawi ya ku Jeffersonville, ndi kumva Njira yoperekedwa ndi Mulungu ya lero. Ndiye inunso mukhoza kunena kuti, “Ndamva za Inu, koma tsopano ndikukuonani inu”.

M’bale. Joseph Branham

Uthenga: 65-1127E Ine Ndakhala Ndikumva Koma Tsopano Ine Ndawona

Malemba

Genesis 17
Eksodo 14:13-16
Yobu chaputala 14 ndi 42:1-5
Amosi 3:7
Marko 11:22-26 ndi 14:3-9
Luka 17:28-30

25-0629 Kuyesera Kuti Umuchitire Mulungu Ntchito Popanda Icho Kukhala Chifuniro Cha Mulungu

Uthenga: 65-1127B Kuyesera Kuti Umuchitire Mulungu Ntchito Popanda Icho Kukhala Chifuniro Cha Mulungu

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mkwatibwi wa Khristu, tiyeni ife tibwere palimodzi Lamlungu 12:00 p.m., nthawi ya ku Jeffersonville, kuti tidzamve 65-1127B Kuyesera Kuti Umuchitire Mulungu Ntchito Popanda Icho Kukhala Chifuniro Cha Mulungu

M’bale. Joseph Branham