26-0315 Malo Osankhidwa Ndi Mulungu A Kupembedza

Uthenga: 65-0220 Malo Osankhidwa Ndi Mulungu A Kupembedza

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Mayi Yesu Khristu,

Tsiku lija ndi Lero. Nthawi ija ndi ino. Mulungu anatumiza mphungu Yake ya mphamvu padziko lapansi kuti idzayitane Mayi Yesu Khristu Wake, kuti alankhule ndi kumuuza kuti, “Inu ndinu AMENE ine ndinasankha. Inu ndinu AMENE ine ndimakukondani.Inu ndinu namwali Mkwatibwi Wanga wa mawu angwiro ,Ife Ndife M’MODZI.”

Kungomva chabe mawu amenewo, mitima yathu imadumphadumpha ndi chisangalalo. Kuganiza, padziko lonse lapansi, ndi ma mamiliyoni ndi mamiliyoni a anthu ake ambirimbiri, pali Mayi Yesu Khristu MMODZI yekha, ndipo INUYO ndinu Iye, amene Iye akubwelera.  

Pali malo AMODZI okha osankhidwa opembedzera. Pali Uthenga UMODZI wokha wosankhidwa wangwiro. Pali MKWATIBWI WANGWIRO MMODZI YEKHA wosankhidwa…NDIPO NDI IFEYO CHIMENECHO!!

Atate ali ndi malo amodzi osankhidwa opembedzera, Ambuye Yesu Khristu; Iye ndiye Mawu. Lero, pali malo amodzi okha omwe imfa ya uzimu siyingakanthe: Mawu. Imfa siyingakanthe Mawu, chifukwa Ndi Mawu Amoyo a Mulungu.

Vumbulutso lonse lathunthu la Mawu Amoyo lavumbulutsidwa kwa Mayi Yesu Khristu okha. Pali malo amodzi okha osankhidwa kumene Mayi Yesu Khristu angapiteko ndikumva Mawu ANGWIRO OLANKHULIDWA. Pali mneneri mmodzi yekha wosankhidwa kukhala Mawu a Mulungu. Pali malo amodzi okha omwe Mayi Yesu angapiteko ndikumva, PAKUTI ATERO AMBUYE: KUKANIKIZA KUSEWERA.

Kudzakhala kuli Kuwala cha mu nthawi ya madzulo, malo okha osankhidwa ndi Mulungu kuti uzipembedzapo. O, kodi Uthenga uwu wafika ku chiyani, kodi Iye achita chiyani? Ndipo mu tsiku lake kudzakhala kuli Kuwala pa nthawi ya madzulo, ndipo (chiyani?) kuti awalandire ana Ake akubwerera kwawo ku Dziko loona lolonjezedwa, ndi chizindikiro chomwe chija cha Lawi la Moto limene linawatsogolera ana a Israeli kudutsa mu chipululu.

Kodi ndimosamala motani momwe Mkwatibwi Wake ayenera kukhalira kuti atsatire ndikumva Liwu la Mwamuna Wake likulankhula naye. Pali malo AMODZI okha omwe ife tingapite ndikukhala otsimikiza handiredi peresenti. Pali Liwu limodzi lokha lomwe ife tayika komwe tikupita Kwamuyaya wathu.

Mayi Yesu Khristu amakhulupirira kuti Mawu omwe iye amamva pa matepi ndi Mawu a Mwamuna Wake.Iye Amakhulupirira kuti Mawu Ake safunikira kutanthauzira. Chifukwa chake, iye amakhulupirira kuti pali malo AMODZI okha operekedwa omwe iye angapite ndi kunena AMENI ku mawu aliwonse.Liwu la Mwamuna Wake pa matepi.

Kamodzinso kena, Mayi Yesu Khristu, ochokera kuzungulira padziko lonse lapansi, akhozanso kunena kuti, “Lero, Mawu awa olankhulidwa, ali kukwaniritsidwa”.

Wokondedwa Mulungu, kutali komwe kuwoloka zipululu uko mu Tucson, kupita mpaka mu California, mpaka mu Nevada ndi Idaho, kupita mpaka cha Kummawa ndi kozungulira, kutsikira mu Texas; pamene kuitanira uku kuli kuperekedwa, anthu atakhala mkati—mu mipingo yaying’ono, malo omwetsera mafuta, mmakomo, akumvetseramo.

Inu muli kuitanidwa kuti mudzamvetsere ndi Branham Tabernacle nthawi ya 12:00 PM, nthawi ya ku Jeffersonville, pamene tikumva Mulungu akulankhula ndi Mkwatibwi Wake wosankhidwa, Uthenga: “Malo Osankhidwa Ndi Mulungu Opembedzera” 65-0220.

M’bale Joseph Branham

Malemba Opatulika: Deuteronomo 16:1 mpaka 3