Uthenga: 65-0219 Lero Lembo Ili Lakwanitsidwa
- 26-0308 Lero Lembo Ili Lakwanitsidwa
- 24-0609 Lero Lembo Ili Lakwanitsidwa
- 22-1113 Lero Lembo Ili Lakwanitsidwa
- 19-0616 Lero Lembo Ili Lakwanitsidwa
Yokondedwa Mbewu Ya chifumu Yapamwamba,
Nthawi yomwe ife takhala tikuyiyembekezera mwachidwi komanso mofunitsitsa ndi ino. Ife tafika.Ife tikuwona iyo ikutambasulidwa pamaso pathu. Tsiku lililonse ulosi ukukwaniritsidwa, ndipo ife tinganene kuti: LERO LEMBA ILI LAKWANIRITSIDWA PA MASO PATHU.
Ndi kukondoweza Kwa Vumbulutso lotani likuchitika ndi mkwatibwi. Ndi Uthenga uliwonse womwe ife timamva, ife timamvelera mkatikati mwa mitima ndi miyoyo yathu, “Kodi izo zingatheke bwanji kukhala
zazikulu mulimosemo komanso zabwino kwambiri, Ambuye?” Kenako Iye amabwera pakati pathu kachiwiri ndikutidzoza ife pamene ife tikumva Mawu Ake akutiitana ife nati, “Inu ndinu Wokondedwa wanga. Ine ndinakusankhani inu kuti mukhale Mkwatibwi Wanga. Monga Ine ndinakulonjezani inu, Ine ndikubwera chifukwa cha Inu. Ine Ndili pa njira yanga. Posachedwapa Ife tidzakhala limodzi ku muyaya.”
Ife tikufuula kuchokera kuzungulira padziko lonse lapansi, tikukwera Kumwamba ndi ma haleluya athu, ma ulemerero, matamando, ndi kulambira kwa Iye. Satana wagonjetsedwa. Atate wachotsa kukayikira kwathu konse, kusatsimikizika kwathu konse, zonse zoganizira. Ife tikhoza kulengeza ndi mtima wathu wonse ndi moyo wathu wonse, Ife NDIFE Mbewu Yachifumu Yapamwamba ya Abrahamu. Mkwatibwi Wachifumu kwa Mwana wa mwamuna Wachifumu wolonjezedwa.
Kukhalapo kwa Ambuye kwakhala kodabwitsa kwambiri pamene Iye akutivumbulutsira Mawu Ake kuposa kale lonse. Iye wagwirizanitsa Mkwatibwi Wake ndi Mawu Ake, natiyika ife mu Maganizo amodzi ndi mgwirizano umodzi ngati gulu limodzi, kumvetsera Liwu La Mulungu likulankhula ndi kutipanga ife kukhala angwiro ndi Mawu Ake.
Uthenga uliwonse umene ife timava uli ngati chitsime cha kasupe chomwe chikuphulika mkati mwa miyoyo yathu; chikutuluka, chikukankhira, ndi kutumphukira kuchokera ku Mpando wa Chifumu wa Mulungu.Ife Tikumwa ndi kumwa ndi kumwa, kuyipangitsanso miyoyo yathu kukhala yatsopano.
Abale ndi Alongo Anga, Ife ndife kukwaniritsidwa kwa Malemba omwe amati Iye adzakhala ndi namwali Mkwatibwi wa Mawu. Ife ndife: Lero Lemba ili lakwaniritsidwa.
Mulungu Mwiniwake analankhula kuchokera Kumwamba kwa mngelo Wake wachisanu ndi chiwiri nati, “Monga Yohane Mbatizi anatumizidwa kuti atsogolere Kubwera koyamba kwa Khristu, Uthenga wako udzatsogolera Kubwera kwa Iye kachiwiri, kudziko lonse lapansi.” Mkwatibwi anganene kuti: Lero Lemba ili lakwaniritsidwa.
Kodi ife tingamvetse kuti Liwu lomwelo la Mulungu lankhulidwa m’masiku athu ano kudzera m’milomo ya munthu, kujambulidwa, kusungidwa, ndi kusungidwira kuti iye athe kulankhula ndi aliyense wa ife, Pakuti Atero Ambuye? Iye wazipanga izo kukhala zotheka kuti ife sitimafunikila kuti tisatenge mawu a wina aliyense, osati malingaliro a wina, osati maganizo a wina, basi kungokhala pansi ndikumamvetsera Liwu Lake likuyankhula mwachindunji kwa ife Mawu Ake Oyera.
KODI CHOMWE CHIKUCHITIKA NDI CHIYANI LERO?
Ndipo M-w-a-n-a wa Mulungu yemweyo amene anabwera kummawa ndi kudzadzitsimikizira Yekha ngati Mulungu wowonetseredwa mu thupi, ndi M-w-a-n-a wa Mulungu yemweyo kumadzulo kwa dziko lapansi kuno, amene akudzizindikiritsa Yekha pakati pa mpingo usikuuno, yemweyo dzulo, lero, ndi kwanthawizonse. Kuwala kwa kumadzulo kwa Mwana kwafika. Lero Lemba ili lakwaniritsidwa pamaso pathu.
KODI IFE TILI MU MCHIFUNIRO CHANGWIRO CHA MULUNGU PAKUNENA NDI KUKHULUPIRIRA: “KUSEWERA MATEPI NDI NJIRA YOPEREKEDWA NDI MULUNGU KWA MKWATIBWI WAKE”?
KODI PALI CHINTHU CHINANSO CHACHIKULU KUPOSA KUMVERA MATEPI?
Nthawizonse mu zitatu, monga ine ndinanenera usiku wathawu, Mulungu amaimiriridwa. Panali anthu Achisodomu, Aloti, ndi a Abrahamu. Izo ziri mmalo omwewo usikuuno, dziko lakhala monga chomwecho.
Zindikirani, Mmodzi amene anatsalira ndi Abrahamu anali Mulungu Mwiniwake. Awiri enawo anali amithenga a Mngelo.
TSONO KODI NDI NDANI YEMWE AKUYANKHULA NDI IFE PA MATEPI?
Ndiroleni ine ndikufunseni inu chinachake. Tayang’anani pa chikhazikitso ichi tsopano. Abrahamu anamutcha Munthu uyu amene ankayankhula ndi iye, “Elohim.” Liwu la Chihebri lakuti Elohim limatanthauza “Wokwanira Zonse Uja, Mmodzi amene ali Wamuyaya,” Elohim, Mulungu Mwiniwake!
KODI NDI KOFUNIKA MOTANI KUKANIKIZA KUSEWERA ?
…“tsiku lina Mzimu Woyera udzabwera ndipo akadzachita chinthu chomwecho, ndipo kudzanena mawu amodzi motsutsa Iwo sadzakhululukidwa nkomwe.” Limenelo ndi tsiku lino, limene Mawu aliwonse ayenera kukhala pamodzi. “Kuyankhula mawu motsutsa Iwo; sichidzakhululukidwa konse mdziko lino kapena dziko likudzalo.”
Ma aleluya athu a sabata yatha ndi kutamanda Ambuye zinali zongokonzekera za zomwe ziti zidzachitike Lamlungu lino, pamene Mkwatibwi akugwirizananso ndikumvetsera MULUNGU akutilimbikitsa ndi kutitsimikizira ife kuti ife ndife osankhidwa Ake, ndipo Iye akubwera posachedwa kuti atitengere ife ku Mgonero Wathu Waukwati waukulu, kenako kwathu kwa mtsogolo.
Ili ndilo tsiku limene AMBUYE adapanga; ife tidzakondwera ndi kusangalala nalo.
M’bale Joseph Branham
Uthenga: 65-0219 – “Lero Lemba Ili Lakwaniritsidwa”
Malemba:
Yohane Woyera Mutu 16
Yesaya 61:1-2
Luka Woyera 4:16