25-0525 Kukhazikitsidwa #4

Uthenga: 60-0522E Kukhazikitsidwa #4

PDF

BranhamTabernacle.org

Okondedwa Iwo Otembenuka,

Mwa Kukanikiza Kusewera, tikumvera Mawu osalephera a Mulungu. Ndi Mawu aliwonse Choonadi, mawu aliwonse a Iwo. Ife tayitanidwa ndi kusungidwa, kudzazidwa ndi kuikidwa pambali; odzazidwa ndi Mzimu Woyera, ndipo tsopano ali kale mu Dziko la Kanani. Sitikuwopa kalikonse … PALIBE, timadziwa kuti ndife ndani.

Chifukwa takhala ndi Mawu Ake, monga anatilamulira, adzatiuza kuti anatisiyira cholowa.  Ndi liti pamene Inu munachita izo, Atate? Pamene Ine ndinakusankhani inu ndi kuika maina anu pa Bukhu la Moyo wa Mwanawankhosa asanaikidwe maziko a dziko.

Pamene chidzalo cha nthawi chinadza, Ine ndinatumiza Yesu Mwanawankhosa, Yemwe anaphedwa kuchokera ku maziko a dziko, kuti inu mukhoze kulandira cholowa chanu kuti mukhale ana Anga aamuna ndi aakazi, milungu ing’onoing’ono.

Ndidayenera kukuyang’anirani inu kuti muone ngati mukunjenjemera ndi malo omasuka ndisanakukhazikitseni.

  • “Kodi inu mukukhulupirira kuti kusewera Liwu Langa pa matepi mu mpingo ndi kulakwa?”
  • “Inde, usamasewere matepi kutchalitchi.”
  • “Zitsutseni izo.
  • “Kodi inu mukukhulupirira Mawu Anga pa matepi akusowa kutanthauzira?”
  • “Inde, pakufunika winawake kuti afotokoze Izo.”
  • “Iwe ukuphokosera, zitulutseni kunja izo . Inu Simunakonzekerebe.” 

Pamene mwakonzeka, mudzati, “Ameni” ku Mawu aliwonse. 

  • “Kodi ukukhulupirira kuti Ine ndine yemweyo dzulo, lero, ndi kwanthawizonse?”
  • “Ameni.”
  • “Kodi inu mukukhulupirira Liwu Langa pa matepi ndilo MAWU OFUNIKA KWAMBIRI omwe inu muyenera kuwamva?” 
  • “Ameni.”
  • “Kodi inu mukukhulupirira Liwu Langa pa tepi lidzagwirizanitsa Mkwatibwi?”
  • “Ameni.”
  • “Kodi mukukhulupirira kuti mngelo Wanga wamphamvu adzakuzindikiritsa iwe kwa Ine?”
  • “Ameni.”

Mukukhala olimba tsopano. Ndakuyang’anani kuti muone ngati muli ndi zingwe komanso malo otayirira. Ndakonzeka kutseka chitseko. Ine ndiyika Chisindikizo Changa pa iwe. Mwadutsa pakuwunika kwanga. 

Tsopano ndiroleni ine ndikuuzeni inu chinachake, Okondedwa Anga anthu ofunika mu maiko a tepi; kutsidya kwa nyanja ndi kulikonse komwe muli, musachite mantha. Zonse zili bwino. Ine ndinakudziwani inu asanaikidwe maziko a dziko. Ndinkadziwa zonse zimene zidzachitike. 

Ine ndikudzerani inu posachedwa ndi kukutengerani inu Kumalo kumene kulibe imfa, kopanda chisoni, kopanda nsanje, kopanda kalikonse; ungwiro basi, chikondi changwiro.
    
Kufikira pamenepo, musaiwale konse, Ine ndikupatsani inu Mawu Anga, iwe NDIWE MAWU ANGA opangidwa thupi. Ngati inu mufuna CHINTHU CHILICHONSE, yankhulani Icho, ndiye mukhulupirireni Icho; Ndi cholowa chanu.

Ine ndikutumiza Liwu Langa kwa inu kachiwiri Lamlungu lino ndi kufotokoza Izo zonse kwa inu. Ndikuwuzaninso kuti ndinu ndani, komwe mukupita, ndi momwe zilili kumeneko, pakali pano.

Bwerani mudzajowine Mkwatibwi Wanga pamene Ine ndikuwapangitsa iwo kukhala limodzi mu malo ammwambamwamba Lamlungu lino pa 12:00 p.m., nthawi ya ku Jeffersonville, ndipo mudzandimvere Ine mwakukukhazikani inu pa malo mwa Mawu Anga.   60-0522E  Kukhazikitsidwa Gawo Lachinayi
   

M’bale. Joseph Branham