Uthenga: 65-0118 Mbewu Ya Chisokonezo
Wokondedwa Mmodzi Wa Iwo,
Momwe anthu akatifunsa ife:
Funso: Kodi inu ndinu m’modzi mwa anthu omwe amakhulupirira kuti Mulungu anatumiza William Marrion Branham kuti adzaitane Mkwatibwi wa Mulungu?
Yankho: INDE, ndine m’modzi wa iwo.
Funso: Inu mumakhulupirira Mawu onse omwe ananenedwa pa matepi awo?
Yankho: Ambuye alemekezeke, ndine m’modzi wa iwo.
Funso: Ndiye muyeneranso kukhulupirira kuti muyenera Kukanikiza Kusewera ndikumva Liwu Lake kuti mukhale Mkwatibwi wa Khristu?
Yankho: Ulemerero, ndine ndendende ameneyo, ndine ameneyo mpaka kufikila mkati…Ndine m’modzi wa iwo.
Funso: Inu mukundiwuza ine, inu mukukhulupiriradi kuti ndinu Mbewu Yake yosankhidwa, yosankhidwiratu, Yachifumu yomwe idakonzedweratu kuchokera ku maziko a dziko lapansi kuti ikhulupirire Mawu Ake, kukhala Mkwatibwi Wake, ndikukhala angwiro pamaso Pake, opanda tchimo lililonse, ndipo simungathe kunyengedwa?
Yankho: Haleluya,inu mwamvetsa, ine ndine ameneyo 110%, INE Ndine Mmodzi Wa Iwo.
Malingana ndi Yesu mwiniwake, ife ndife kutanthauzira kwa Mawu Ake. Ana a Ufumu. Kuwonetseredwa kwa Mzimu Woyera. Mbewu ya Ufumu ya nthawi ino.
Mukudziwa chiyani? Yakwana nthawi yoti aliyense adziwe bwino lomwe kuti palibe cholakwika.Ife timalola Mulungu kulankhula kudzera mwa mneneri wake ndikuyika izo zonse pamodzi kwa inu.
Mphamvu yomweyo yomwe inalankhula dziko lapansi kuti likhalepo ili mwa anthu omwe ali ndi Mzimu Woyera. Ndizo kulondola. Amuna ndi akazi, ndi nthawi yoti ife tipeze kuti Inu ndinu ndani_ . Mdierekezi akuyesera kukubisani inu kumbuyo, kukuuzani inu kuti ndinu kanthu kena konyozeka. Inu simuli.Inu ndinu ana aamuna ndi akazi a Mulungu.
UMulungu siwuli Kumwamba, wuli mwa inu. Haleluya!
Yankho: Mulungu sali Kumwamba, akukhala ndi moyo mwa aliyense wa ife!
Ndi tsiku lililonse latsopano, ndi mpweya uliwonse womwe ife timapuma, Vumbulutso lomwe watipatsa la yemwe ife tili limakhala likukula ndi kukula. Ndife Mawu amoyo okhala m’thupi.
Tikudziwa izi chifukwa watipatsa Vumbulutso limene Iye anatumiza m’masiku athu ano; amene Mulungu mwiniwake anati adzatumiza kuti akalalikire ndi kuphunzitsa Mawu Ake mu Chivumbulutso 22.
Ine Yesu ndatumiza mngelo wanga kudzachitira umboni kwa inu zinthu izi mmipingo.
Iye anatumiza mngelo Wake: William Marrion Branham, kuti akalankhule m’mipingo YAKE…Izo mnzanga zikutanthauza KUSEWERA MATEPI M’MIPINGO YANU. Zimenezo sizitengera vumbulutso mkomwe, inu muyenera kungowerenga.
Malingana ndi Mawu, ino ndi nthawi yonyenga kwambiri mu mbiri ya dziko lapansi. Mzimu wa chowonadi ndi wabodza udzakhala moyandikana kwambiri moti ukanadzanyenga osankhidwa omwe ngati n’kotheka.
Mulungu anatumiza Mngelo WAKE ku mipingo. Ife tili ndi Liwu Lake kusonga ya zala zathu. Ife tikhoza kumva ndendende Mawu pa Mawu omwe Iye analankhula. Izo Sizikusowa kufotokozera kapena kutanthauzira, chomwe Mkwatibwi ayenera kuchita ndi kokha KUNGOKANIKIZA KUSEWERA NDI KUKHULUPILIRA.
Iye anatichenjeza ife, musasinthe kolemba kamodzi kapena dontho limodzi pa matepi. Musayike kumvetsetsa kwanu kapena malingaliro anu, ingomverani Liwu Langa ndikukhulupirira. Mpaka lero, izo zakhala zisakukhala zotheka; koma lero ndi chifukwa chakuti ndi njira yoperekedwa ndi Mulungu lero.
Tangomva kumene Mibadwo Isanu ndi iwiri ya Mpingo ndi momwe m’badwo uliwonse, pamenepo panabuka nimizimu imeneyo kuti ichotse anthu ku Mawu owona. Momwe mu m’badwo uliwonse, mthenga atachoka, zomwe iwo ankachita kuti atengere anthu ku kukachikhulupiliro kapena mbalume; kwa iwo eni ndi ku lingaliro la munthu.
Lero akuyesera kupha chikoka chathu ndikuti, “O, iwo amakhulupirira kuti matepi ndi Liwu lofunikira kwambiri lomwe muyenera kumva. Inu muyenera kusewera matepi mu mpingo wanu … ndizopanda pake. M’bale Branham sananene kuti sewerani matepi mu mpingo. Tsopano ndi liwu la utumiki lomwe inu muyenera kumva.”
Kwa ine, imeneyo ndi mbewu ya chisokonezo! INU MUYENERA KUKANIKIZA KUSEWERA ndikumva Liwu la Mulungu m’mipingo yanu chifukwa Ndilo Liwu LOKHALO lomwe linatsimikizilidwa ndi Mulungu Mwiniwake.Inu muyenera kumvera Mawu onse omwe Mulungu analankhula.
Ine Yesu ndatumiza mngelo wanga kudzachitira umboni kwa inu zinthu izi mmipingo.”
Mngelo wotsimikiziridwa uja amalankhula mu Tchalitchi chathu, motero ine ndikukuitanani inu kuti mudzabwere kulumikizana nafe kudzava Liwu limenelo ndi Mkwatibwi Wake kuchokera kuzungulira padziko lonse lapansi pa 12:00 PM, nthawi ya ku Jeffersonville, ndi kudzamva: 65-0118 – “Mbewu ya Chisokonezo”.
M’bale Joseph Branham