CHIDZIWITSO CHAPADERA

Wokondedwa Mkwatibwi,

Ambuye wayika pamtima wanga kukhala ndi Uthenga Wapadera ndi Utumiki wa Mgonero pa Madzulo a Chaka Chatsopano kachiwiri chaka chino. Ndi chinthu chachikulu chiti chimene tingachite, abwenzi, kuposa kumva Liwu la Mulungu likulankhula kwa ife, kutenga nawo mbali pa Mgonero wa Ambuye, ndi kuperekanso miyoyo yathu ku utumiki Wake pa kulowa mu m’Chaka Chatsopano. Idzakhala nthawi yopatulika bwanji kutsekera dziko kunja, ndi kulumikizana ndi Mkwatibwi pa kusonkhana kwapadera kumeneku mu Mawu, pamene tikunena kuchokera mu mitima yathu, “Ambuye, tikhululukireni ife zolakwa zathu zonse zomwe takhala tikuchita chaka chonse; tsopano tikuyandikira kwa Inu, ndikufunsani ngati mudzatigwira dzanja ndi kutitsogolera chaka chomwe chikubwerachi. Mulole ife tikutumikireni Inu kuposa kale lonse, ndipo ngati icho chiri mu Chifuniro Chanu Chaumulungu, mulole icho chikhale chaka cha Mkwatulo waukulu umene uti uchitike. Ambuye, ife tikungofuna kuti tipite Kwathu kukakhala ndi Inu mu Muyaya.” Ine Sindili onyalanyaza kudikira kusonkhana mozungulira Mpando wachifumu Wake ku msonkhano wapadera wodziperekanso uwu, alemekezeke Yehova.

Kwa okhulupilira okhala mu dera la Jeffersonville, Ine ndikufuna kudzayamba tepi nthawi ya 7:00 pm pa nthawi ya kwathu kuno. Uthenga wonse ndi Mgonero udzakhala pa Wailesi ya Liwu panthawiyo, monga tinachitira m’mbuyomu. Tidzakhala ndi mapaketi a vinyo a Mgonero omwe adzapezeke Lachitatu, pa Disembala 18, kuyambira 1:00 – 5:00 pm, kuti mudzawatengere ku nyumba ya YFYC.

Kwa inu amene mumakhala kunja kwa dera la Jeffersonville, chonde khalani ndi chiyanjano chapadera chimenechi panthawi yomwe ndi yabwino kwa inu kwanuko. Tidzakhala nayo linki yotengera Uthenga ndi Chiyanjano cha Mgonero posachedwapa.

Pamene tikuyandikira Tchuthi cha Khrisimasi, ndikufuna ndikufunireni inu ndi banja lanu Nyengo ya Tchuthi YABWINO NDI YOTETEZEKA, ndi Khrisimasi yabwino, yodzaza ndi chisangalalo cha Ambuye Yesu woukitsidwayo… LIWU.

Mulungu akudalitseni,

M’bale Joseph

Gwero: https://branhamtabernacle.org/en/bt/F6/110067