26-0104 Zitsime Zong’aluka

Uthenga: 64-0726E Zitsime Zong’aluka

PDF

BranhamTabernacle.org

Okondedwa Iwo Omwa Pa Chitsime Cha Kasupe

Ndi Khirisimasi ndinso Zaka za tsopano zotani zomwe ife takhala tili nazo. Talandira ndikutsegula mphatso za Mulungu zomwe adatumiza kwa Mkwatibwi Wake. Mphatso yathu yoyamba inali Mphatso yayikulu kwambiri ya Khirisimasi yomwe idakulungidwapo. Mulungu Mwiniwake adakulunga Iye mwini mu thupi la munthu ndipo adatumiza phukusi limenelo kudziko lapansi. Inali Mphatso Yake yoyamba yayikulu yobwezeretsa Mkwatibwi Wake.

Kenako Mulungu adatumiza phukusi lina lalikulu kwa Mkwatibwi Wake. Iye Anatikonda ife kwambiri kotero kuti Iye anabwera nadziulula Yekha mu thupi kachiwiri kuti Iye athe kulankhula nafe pakamwa ndi Kupita ku khutu. Anafuna kuti Iye ndi Mkwatibwi Wake akhale Mmodzi.

Ndipo tsopano, abwenzi, musati mundive ine molakwika.Ine nditi ndinene izi ndi ulemu mumtima mwanga, podziwa kuti ndine munthu womangirilidwa ku Kumuyaya amene ndidzayima mu mchiweruzo tsiku lina: Anthu zikwizikwi akuyiphonya mphatso yawo. Mukuona? Iwo sangathe kuyimvetsa iyo. Ndipo iwo akuyiyang’ana, ndipo nanena, “O, iye ndi munthu chabe.” Izo Ndi zoona. Kodi iye anali Mulungu kapena Mose amene anapulumutsa anthu? Iye anali Mulungu mwa Mose. Mukuona? Iwo Analirira kwa mpulumutsi. Ndipo pamene Mulungu anatumiza mpulumutsi kwa iwo, iwo analephera kuchiwona icho, chifukwa icho chinali mwa munthu, koma sanali munthuyo, anali Mulungu mwa munthuyo.

Lero, kachiwiri, anthu zikwizikwi akuyiphonya mphatso yawo ndipo akunena kuti, “Inu simukuyenera kumvera matepi, tsopano pali amuna ena odzozedwa,” zomwe ndi zoona, koma iwo akulephera kuzindikira kuti ilo ndi Liwu LOKHALO lotsimikiziridwa ndi Mulungu , likulankhula Pakuti Atero Ambuye kudzera mwa munthu ameneyo. Liwu limenelo ndi Yurimu Tumimu wa Mulungu, Mtheradi Wake wa lero.

Pamene ife tikumvetsera Liwu Lake pa matepi ife kwenikweni timakhala kuti tikumwa kuchokera ku Chitsime cha Kasupe wa Mulungu, chomwe sichifuna sichifuna kupopa, sichifuna kukoka, sichifuna kujoyina, kapena sichifuna kugwedeza; ife tikungokhulupirira ndi kupumula pa Mawu aliwonse olankhulidwa.

Pa kumvetsera Liwu limenelo pa matepi, malingana ndi Yesu Mwiniwake, ife tili nawo umboni weniweni wa Mzimu Woyera mtsiku lathu.

Kotero pamenepo pali umboni weniweni wa Mzimu Woyera! Iye sanayambe wandiuzapo ine chirichonse cholakwika panobe. Iwo, “Uli umboni wa Mzimu Woyera, ndi iye yemwe angakhoze kukhulupirira Mawu, ngati inu mungakhoze kuwalandira Iwo.

Mulungu wapereka Kasupe amene ife tingamwe kuchokera Kwa iye mphindi iliyonse ya tsiku lililonse. Nthawi zonse amakhala watsopano. Si chinthu chinachake choyima, Iye ndi Kasupe Wake wosaguga, wodzithandizira yekha; inu mukungoyenera Kukanikiza kungosewera.

Kunena za MPHATSO yochokera kwa Mulungu, kodi inu mungaganizire momwe Mphatso iyi kwenikweni ili YAIKULU? Mu mkuphweka pa Kukanikiza kungosewera ndi kumvetsera ku Liwu Lake pa matepi, ndiye lokhalo…LIWU LOKHALO padziko lapansi lomwe inu simukufunaso fyuluta, sefa, kapena china chilichonse.Inu muyenera kungomvetsera, kukhulupirira, ndi kunena ameni ku Mawu onse.

Mulungu mwiniwake wapereka njira iyi, NJIRA YAKE YOKHAYO, yolandililako moyo wosatha, komanso ngakhale chofunika kwambiri, KUKHALA MKWATIBWI WAKE. Tikhoza kungogona pachifuwa Chake ndi kuyamwa mphamvu zathu pomvera Kasupe Wake, Liwu Lake, El Shaddai akulankhula ndi Mkwatibwi Wake.

Chaka chino chikhale chaka chomwe Iye akubwera kwa ife, Mkwatibwi Wake wokondedwa. Ife Tikuyang’anira ndi kuyembekezera ndi chiyembekezo chachikulu. Tsiku lililonse tsopano tidzayang’ana omwe takhala tikulakalaka kuwawona akuwonekera. Ife Tidzazindikira, mu mkutwanima Kwa diso chabe, kuti tidzachoka pano, kuyitanidwa ku Mgonero Wathu wa Ukwati.

Ambuye, pamene ife tidzawona gome lalikulu ilo litayikidwa kunja uko, ku mgonero umenewo, mailosi zikwi utali wake; kuyang’anizana pa gomelo kwa wina ndi mzake, ankhondo akale a zipsyera, misozi ya chimwemwe ikutsikira pansi pa masaya athu. Mfumu kutulukira uko, kukongola Kwake, chiyero, kuyendera pansi motsatira gomelo, ndi kutenga manja Ake Omwe ndi kumaipukuta misonzi kuichotsa pa maso awo, akuti, “Musati muziliranso. Zonse zatha. Lowani mu zisangalalo za Ambuye.” Zovutikira za ulendo sizidzawoneka ngati kanthu pamenepo, Atate, pamene ife tidzafika pa mapeto a ulendo.

Bwerani ndipo mudzamwe, mudzamwe ndipo mudzamwe kuchokera ku Kasupe woperekedwa ndi Mulungu lero ndi ife Lamlungu lino nthawi ya 12:00 PM, nthawi ya ku Jeffersonville. Iwo ndi malo okhawo omwe inu mungathe kupumulirako mokwanira ndikunena AMEN ku Mawu aliwonse omwe mukumva. Ndi chitsime chake cha Kasupe choperekedwa kwa Mkwatibwi Wake kuti amwe kuchokera ku icho.

M’bale Joseph Branham

Uthenga: 64-0726E Zitsime Zong’aluka
Malemba oti muwerenge musanamve Uthenga:
Masalmo 36:9
Yeremiya 2:12-13
Yohane Woyera 3:16
Chivumbulutso Mutu 13