25-1221 Kupita Kuseri Kwa Msasa

Uthenga: 64-0719E Kupita Kuseri Kwa Msasa

PDF

BranhamTabernacle.org

Wokondedwa Wachikondi,

Mulungu samasintha. Mawu Ake samasintha. Pulogalamu yake simasintha. Ndipo Mkwatibwi Wake samasintha, Ife tidzakhala ndi Mawu. Iwo ndi oposa moyo kwa ife; iwo ndi Kasupe wa Madzi amoyo.

Chinthu chokha chomwe ife tapatsidwa ntchito ndikumva Mawu, omwe ndi Mawu a Mulungu otsimikiziridwa omwe adajambulidwa ndikuyikidwa pa matepi. Chinthu chokha chomwe timawona si chikhulupiriro, osati gulu la amuna, sitiwona china chilichonse koma Yesu, ndipo Iye ndiye Mawu opangidwa kukhala thupi mu masiku athu ano.

Mulungu ali mu Msasa wathu ndipo tili panjira yopita ku Ulemerero motsogozedwa ndi Lawi la Moto, lomwe ndi Mulungu Mwiniwake akulankhula kudzera mwa mneneri wake wotsimikiziridwa wa Malaki 4. Tikudya Mana wobisika, Madzi amoyo omwe Mkwatibwi yekha ndi amene angadye.

Mulungu sasintha njira zake, koteroso mdierekezi sasintha njira zake. Zimene adachita zaka 2000 zapitazo, akuchita zomwezo lero, kupatula kuti ali wa mphavu kwambiri.

Tsopano, zitatha zaka foro handiredi, Mulungu anadzayenda kumene pakati pawo tsiku lina. Molingana ndi Lemba, Iye anali woti adzasandulike thupi ndi kudzakhala pakati pawo. “Dzina Lake azidzatchedwa Wauphungu, Kalonga wa Mtendere, Mulungu Wamphamvu, Atate Wosatha.”
Ndipo pamene Iye anadzabwera pakati pa anthuwo, iwo anati, “Ife sitimulola kuti Munthu uyu azitilamulira ife!

Potengela ndi Malemba, Mwana wa Munthu adzabweranso ndi kukhala ndi moyo ndi kudziulula Yekha mu thupi la munthu, ndipo Iye anachitadi zimenezo, ndipo iwo akunena zomwezo. Inde, iwo amakamba mobwereza ndi kulalikira Uthenga, koma Iwo samalola munthu ameneyo kuwalamulira iwo.

Izi ndizo kwenikweni zomwe zili kuchitika :

Ndipo monga zinaliri kumeneko, chomwechonso izo ziri tsopano! Baibulo linati mpingo wa Laodikaya ukanadzamuika Iye panja, ndipo Iye anali akugogoda, akuyesera kuti alowe mkati. Pali chinachake cholakwika penapake.
Tsopano, bwanji? Iwo anali atapanga msasa wawo wawo.

Munthu anganene kuti, “Ine ndikudziwa ndipo ine ndimakhulupirira kuti M’bale Branham anali mneneri. Iye anali mngelo wachisanu ndi chiwiri. Iye anali Eliya. Timakhulupirira Uthenga uwu. Kenako iye ndikupanga mtundu wina wakunyozela, Iwo angakhale uliwonse womwe ulipo, osasewera Liwu LOKHA LOTSIMIKIZILIDWA la Mulungu mu mpingo wawo… Pamenepo pali chinachake cholakwika penakwake. Tsopano, ndi chifukwa chiyani? Iwo adapanga msasa wawo.

Ine ndikunena zinthu izi kuti osati kuti tilekanitse mpingo iyayi, Mawu a Mulungu ndi emene amachita zimenezo. Ine ndikufuna kuti ife tonse tigwirizane pamodzi, tikhale CHINTHU CHIMODZI wina ndi mnzake komanso ndi Iye, koma pali njira imodzi yokha yochitira zimenezo: mozungulira Liwu la Mulungu pa matepi. Ameneyo ndiye PAKUTI ATERO AMBUYE YEKHA WA MULUNGU.

Mulungu wavumbulutsira njira Yake yangwiro kwa ife. Iyo ili yaulemerero kwambiri ndiposo yosavuta. Uthenga uliwonse umene timamumva Iye akutiuza, kutitsimikizira, kutilimbikitsa, kuti NDIFE MKWATIBWI WAKE. Tili mu chifuniro Chake changwiro. Tadzipanga ife eni kudzikonzekeretsa tokha pa KUMUNVA IYE

Uthenga uwu uli watsopano kwambiri kuposa nyuzipepala ya mawa. Ndife ulosi womwe ukukwaniritsidwa. Ndife Mawu owonetseredwa. Mulungu amatitsimikizira ndi Uthenga uliwonse umene timamva kuti tsiku ili lero , Lemba ili likukwaniritsidwa.

Pakhoza kukhala ena uko kudutsa mafuko, kuzungulira dziko, amene ngakhale tepi iyi idzakawapeza mmakomo mwawo kapena mmatchalitchi mwawo. Ife tikupemphera, Ambuye, kuti pamene msonkhano ukupitirira, pa—pa…kapena tepiyo izikaseweredwa, kapena pamalo amene tingadzakhale tiripo, ka—kapena chikhalidwe, mulole Mulungu wamkulu wa Kumwamba mulemekeze kudzipereka uku kwa mitima yathu mmawa uno, ndipo muchiritse osowa, mupereke kwa iwo zimene iwo akuzisowa.

Dikirani chabe mwa ka mphindi ….Kodi Liwu la Mulungu kwa dziko lapansi linalosela ndi kunena chiyani?….anthu azizasewera matepi m’nyumba zawo kapena m’matchalitchi awo.

Koma ife tikutsutsidwa ndi kudzudzulidwa ponena kuti ife SITINGAKHALE NDI Tchalitchi cha Tepi Cha mnyumba? Kodi M’bale Branham sananenepo kuti muzisewera matepi m’matchalitchi anu?

ULEMERERO KWA MULUNGU, IMVETSENI IYO, WERENGENI IZO, IZO NDI PAKUTI ATERO AMBUYE. Ndipo sikuti Iye anangonena izi zokha, komanso posewera matepi m’nyumba zanu ndi m’matchalitchi, Mulungu wamkulu wa Kumwamba adzalemekeza kukhulupirika kwa mitima yathu ndikuchiritsa osowa ndikutipatsa ife CHILI CHONSE CHOMWE TIKUFUNA!!

Chobwerezedwa ichi chimodzi chokhachi CHIKUTSIMIKIZIRA kuti anthu akumvetsera abusa awo ndipo iwo SAKUMVA MAWU, kapena Iwo angawatsutse ndikuwatsimikizira ndi MAWU kuti ife tili mu CHIFUNIRO CHAKE CHANGWIRO, ndipo ndi CHIFUNIRO CHAKE CHANGWIRO KUSEWERA MATEPI M’MATCHALITCHI AWO.

Sindikusokeretsa kapena kubwereza mawu molakwika Mawu monga momwe ambiri amanenera. Imvereni ndipo muwerenge izo nokha.

Ndipo ndi zophweka komanso zangwiro, INGOKANIKIZANI KUSEWERA ndipo mumve Liwu la Mulungu likulankhula nanu. Nenani “Amen” ku Mawu aliwonse omwe inu mukumva. Inu Simuyenera konse kuwamvetsa, inu muyenera kokha kungokhulupilira izo.

“Ine ndikufuna kuti ndipite opanda msasa. Ziribe kanthu kuti ine ndilipira chiyani, ine nditenga mtanda wanga ndipo ndiziunyamula iwo tsiku ndi tsiku. Ine ndipita mopitirira msasa. Ziribe kanthu kuti anthu azinena chiyani za ine, ine ndikufuna kuti ndizimutsatira Iye kunja kwa msasa. Ine ndakonzeka kuti ndizipita.”

Bwerani ndipo mudzapite mopitilira chotchinga cha mawu kupita ku Mawu a Mulungu Lamlungu lino nthawi ya 12:00 PM, nthawi ya ku Jeffersonville. Izo zilibe malire zomwe Mulungu angachite ndiso zomwe adzachita ndi munthu amene ali wokonzeka kupita mopitirira msasa wa anthu.

M’bale Joseph Branham

Uthenga: 64-0719E Kupita Mopitilira Msasa

Malemba Opatulika: Ahebri 13:10-14 / Mateyu 17:4-8