25-0406 Chisindikizo Chachinai

Uthenga: 63-0321 Chisindikizo Chachinai

PDF

BranhamTabernacle.org

Okondedwa Oyera Obadwira Kumwamba

Atate akutisonkhanitsa ife palimodzi mwa Mawu Ake, ndipo kutsimikizira kwa Vumbulutso limenelo kuli kutipatsa ife kukondoweza. Iye anatisankha ife asanaikidwe maziko a dziko, chifukwa Iye ankadziwa kuti ife tikanakhala okhulupirika ku Mawu Ake mwa kusankha kwathu komwe.

Ndiroleni ine ndinene izo kachiwiri kuti izo zilowerere mwakuya kwenikweni. Iye anayang’ana mu nthawi yonse, mpaka mapeto a nthawi zonse, ndipo ANATIONA IFE…kodi inu mukumva zimenezo? IYE ANAKUONA IWE, IYE ANANDIONA INE, ndipo anatikonda ife, chifukwa mwa kusankha kwathu komwe, ife tikanati TIKHALE NDI MAWU AKE.

Pomwepo, Iye ayenera kuti anasonkhanitsa angelo Ake onse ndi akerubi ndi kutilozera kwa ife ndi kunena kuti: “UYO NDI IYE,” “UYO NDI MKWATIBWI WANGA,” “IWO NDIWO AMENE INE NDAKHALA NDIKUWAYEMBEKEZERA!

Monga Yohane, ndicho chifukwa ife tikuchita kufuula konse uku ndi kukuwa, ndi kutamanda Ambuye, ife takondowezedwa pa Vinyo Watsopano ndipo Ife tikudziwa, MOSAKAYIKILA, IFE NDIFE Mkwatibwi Wake.

Zili ngati mvula yonse ndi mikuntho yomwe takhala nayo muno mu Jeffersonville sabata ino…Ifenso tikutumiza CHENJEZO ku dziko.

Mkwatibwi akukhala ndi Bingu la VUMBULUTSO, NDIPO IZO ZIKUPANGA KUSEFUKURA KWAMPHAVU KWA VUMBULUTSO. MKWATIBWI WADZIKONZEKERETSA YEKHA NDI KUZINDIKIRA YEMWE IWO ALI . PITANI MUM’CHITETEZO MOFULUMIRA. KANIKIZANI SEWERANI KAPENA MUWONONGEDWE.

Ife Sitikukhala mu M’badwo wa Mkango, kapena M’badwo wa Ng’ombe, kapena M’badwo wa Munthu; ife tikukhala mu M’BADWO WA Mphungu, ndipo Mulungu watitumizira ife mphungu yamphamvu, Malaki 4, kuti iitane ndi kutsogolera Mkwatibwi Wake.

Zidzakhala zoyenera bwanji Lamlungu lino, pamene Ife tidzakhala olumikizana pamodzi kumvetsera Chisindikizo Chachinai. Lidzakhala Tsiku la Kubadwa kwa mphungu ya mphavu mneneri wa Mulungu.

Tiyeni tikondwerere tsiku lodabwitsali ndikuthokoza Ambuye chifukwa chotitumizira Ife mthenga wake wa chiwombankhanga, amene anamutuma kuti atiitane Ife ndi kutiululira Ife Mau Ake.

M’bale. Joseph Branham

Uthenga: Chisindikizo Chachinai 63-0321
Nthawi: 12:00 PM, nthawi yaku Jeffersonville
Malemba oti muwerenge pokonzekera.

Mateyu Woyera 4
Luka Woyera 24:49;
Yohane Woyera 6:63
Machitidwe 2:38
Chivumbulutso 2:18-23, 6:7-8, 10:1-7, 12:13, 13:1-14, 16:12-16, 19:15-17
Genesis 1:1
MaSalimo 16:8-11
2 Samueli 6:14
Yeremiya 32
Yoweli 2:28
Amosi 3:7
Malaki 4