Okondedwa Iwo Akupumula,
Ili ndilo Dzinja labwino kwambiri m’miyoyo yathu. Kudza kwa Ambuye kuli pafupi kumene. Ife tasindikizidwa ndi Mzimu Woyera; Chisindikizo cha Mulungu cha chivomerezo chakuti zonse zimene Kristu anafera ndi zathu.
Ife tsopano tiri ndi chikole cha cholowa chathu, Mzimu Woyera. Icho ndi Ndichitsimikizo, malipiro ochepera, kuti talandiridwa mwa Khristu. Ife tikupumula mu malonjezo a Mulungu, tikugona mu kutentha kwa Dzuwa Lake lowala; Mawu Ake otsimikiziridwa, kumvetsera ku Liwu Lake.
Ndicho chikole cha chipulumutso chathu. Ife Sitikudandaula ngati tipita Kumeneko kapena ayi, IFE TIKUPITA! Kodi tikudziwa bwanji zimenezi? Mulungu ananena chomwecho! Mulungu analonjeza ndipo ife tiri nacho chikole. Ife talandira kale Icho ndipo Khristu watilandira ife.
Palibe njira yothawira kwa Izo…m’malo mwake, tiri kumeneko! Zomwe tiyenera kuchita ndikungodikira; Iye ali pansi akuchita Chiwombolo Chachibale pakali pano. Ife tiri nacho chikole chake pakali pano. Ife tikungoyembekezera nthawi imene Iye abwereso Kwa Ife. Kenako, m’kamphindi, m’kuthwanima kwa diso tonse tidzapita ku Phwando la Ukwati.
Kungoganizira zonse zimene zili pa tsogolo pa ife. Malingaliro athu sangatengere zonse mkati. Tsiku ndi tsiku Iye akuwulula zambiri za Mawu Ake, kutsimikizira kuti malonjezo aakulu awa ndi athu.
Dziko likugwa; moto, zivomezi, ndi chipwirikiti kulikonse, koma amakhulupirira kuti ali ndi mpulumutsi watsopano amene adzapulumutsa dziko lapansi, ndikubweretsa m’badwo wawo wagolide. Talandira kale Mpulumutsi wathu ndipo takhala tikukhala mu nyengo yathu ya M’badwo wa Golide.
Tsopano Iye akutikonzekeretsa ife ku Chibvumbulutso chochuluka pamene ife tikulowa mu mutu wa Fayifi wa Chivumbulutso. Iye akukhazikitsa chochitika apa cha kutsegula kwa Zisindikizo Zisanu ndi ziwiri. Monga momwe iye anachitira mu mutu 1 wa Chivumbulutso, kutsegula njira ya Mibadwo Isanu ndi iwiri ya Mpingo.
Kodi zina zonse za Dzinja zidzakhala bwanji kwa Mkwatibwi? Tiyeni tiwone mwachidule:
Tsopano, ndilibe nthawi. Ine Ndazilemba izo pano. nkhani ina pa izo apa, koma msonkhano wathu wotsatira ife tisanalowe mu izi mwinamwake pamene ine ndidzachoka kutchuthi changa kapena nthawi ina, ine ndikufuna kuti nditenge masabata makumi asanu ndi awiri awa a Daniele ndi kumangiriza izo mkati momwe muno, ndi kuzisonyeza izo pamene izo zitengera izo ku chisangalalo cha Chipentekoste, ndi kuzibweretsa izo m’mbuyo kumene ndi miliri isanu ndi awiri iyo Zisindikizo Zisanu ndi ziwiri kuti zitsegulidwe pano ife tisanapite, ndi kusonyeza kuti izo ziri pa mapeto, izi…
Ndi nthawi yodabwitsa bwanji yomwe Ambuye wasungira Mkwatibwi Wake. Kudzivumbulutsa Yekha mu Mawu Ake kwa ife kuposa kale. Kutilimbikitsa kuti ndife osankhidwa ake amene Iye akuwadzera. Kutiuza ife kuti tiri mu chifuniro Chake Changwiro pakukhala ndi Liwu Lake, ndi Mawu Ake.
Kodi tikuchita chiyani? Osati chinthu chimodzi, Kungopumula! Kudikirira! Palibenso ntchito zolemetsa, palibenso zokhumudwitsa, TIKUPUMULA PA IZO!
Bwerani mudzapumule nafe Lamlungu lino pa 12:00 p.m., nthawi ya mu Jeffersonville, pamene ife tikumva Liwu la Mulungu LOTSIMIKIZILIDWA likutibweretsera ife Uthenga:
61-0618 – “Chivumbulutso, Mutu Fayifi Gawo II”.
M’bale. Joseph Branham