Uthenga: 61-0108 Chibvumbulutso, Mutu Foro Gawo III
- 25-0112 Chibvumbulutso, Mutu Foro Gawo III
- 21-0103 Chibvumbulutso, Mutu Foro Gawo III
- 16-0417 Chibvumbulutso, Mutu Foro Gawo III
Okondedwa Akumuyaya,
Ndi nthawi yoti tivule chovala chathu chankhondo ndi kuvala kuganiza kwanu kwa uzimu, chifukwa Mulungu akukonzekera kuti amupatse Mkwatibwi Wake Vumbulutso lochuluka la Mawu Ake.
Iye adzakhala akuvumbulutsa kwa ife zinsinsi zonse zakale. Iye adzatiuza zimene zidzachitike m’tsogolo. Zomwe ena onse m’Baibulo adangowona kapena kumva, Iye adzawulula tsatanetsatane wa chilichonse chaching’ono cha Mawu Ake ndi tanthauzo lake kwa ife.
Tidzamva ndi kumvetsa tanthauzo la zizindikiro za m’Baibulo: Zolengedwa Zamoyo, Nyanja Yagalasi, Mkango, Mwana wa Ng’ombe, Munthu, Mphungu, Mpando Wachifundo, Alonda, Akuluakulu, Ma liwu, Chirombo Chakuthengo Chosawetedwa, Zorengedwa za Moyo.
Tidzamva ndikumvetsetsa zonse za alonda a Chipangano Chakale. Yuda: Mlonda wa Kum’maŵa; Efraimu: Mlonda Wa Kumadzulo; Rueben: Mlonda waku Mmwela; ndi Dani: Mlonda wa Kumpoto.
Palibe chimene chikanakhoza kubwera paliponse mozungulira mpando wachifundo umenewo popanda kuwoloka mafuko amenewo. Mkango, luntha la munthu; Ng’ombe: kavalo wantchito; Mphungu: Kuthamanga kwake.
Momwe Kumwamba, dziko lapansi, pakati, ndi pozungulira, iwo anali alonda. Ndipo pamwamba pake panali Lawi la Moto. Palibe chinakhudza mpando wachifundo uwo popanda kudutsa mafuko amenewo.
Tsopano pali alonda a Chipangano Chatsopano: Mateyu, Marko, Luka ndi Yohane, kupita molunjika patsogolo. Chipata chakum’maŵa chimayang’aniridwa ndi mkango, chipata chakumpoto chimayang’aniridwa ndi chiwombankhanga chowuluka, Yohane, m’vangeri. Ndiye sing’anga wa mbali iyi, Luka, munthuyo.
Mauthenga anai a Uthenga Wabwino amateteza Madalitso a Chipentekoste ndi Lemba lirilonse kukhalira khonde ndendende zomwe iwo ananena. Ndipo tsopano Machitidwe a atumwi akuwonetsera lero ndi Mauthenga anai kuti Yesu Khristu ali yemweyo dzulo, lero, ndi nthawizonse.
Pamene wodzozedwa woona wa Mulungu ayankhula, Ilo ndi Liwu la Mulungu! Ife tikungofuna kufuula, “Woyera, woyera, woyera, kwa Ambuye!”
Palibe basi njira yopitira kutali kwa Icho. Ndipotu, ife sitingathe kuchoka kwa Icho, chifukwa Icho sichingatichokere kwa ife. Ndife odindidwa chisindikizo mpaka tsiku la chiombolo chathu. Palibe mtsogolo, palibe kalikonse, zowopsa, njala, ludzu, imfa, kapena CHINTHU, chimene chingatilekanitse ife ku chikondi cha Mulungu chimene chiri mwa Khristu Yesu.
Asanaikidwe maziko a dziko maina athu anayikidwa pa Bukhu la Moyo wa Mwanawankhosa kuti tiwone Kuwala UKU, kulandira Liwu Ili, kukhulupirira Uthenga Uwu, kulandira Mzimu Woyera wa tsiku lathu ndi kuyenda mwa Iwo. Pamene Mwanawankhosa anaphedwa, MAYINA ATHU anayikidwa pa Bukhu pa nthawi yomweyo Dzina la Mwanawankhosa linayikidwa pamenepo. ULEMERERO!!
Kotero, palibe chimene chingatilekanitse ife ku Uthenga uwu. Palibe chimene chingatilekanitse ife ku Liwu limenelo. Palibe chimene chingatenge Vumbulutso la Mawu Awa kwa ife. Ndi zathu. Mulungu anatiyitana ife ndipo anatisankha ife ndipo anatikonzeratu ife. Zonse ndi za Ife, Ndi zathu.
Pali njira imodzi yokha yopezera zonsezi. Inu Mukuyenera kutsukidwa ndi madzi a Mau. Inu mukuyenera kumva Mawu inu musanalowe mmenemo. Ndipo pali njira imodzi yokha imene inu mungafikire kwa Mulungu, ndiyo mwa Chikhulupiriro. Ndipo Chikhulupiriro chimadza pakumva, kumva Mawu a Mulungu, amene akunyezimiritsidwa kuchokera ku Malo Opatulikitsa kupita kwa mthenga wa m’badwowo.
Kotero, apa, mngelo wa m’badwo wa mpingo akunyezimira m’madzi awo Yemwe Munthu uyu ali muno, akunyezimiritsa chifundo Chake, Mawu Ake, chiweruzo Chake, Dzina Lake. Zonse zikuwonetseredwa muno pamene inu mumalekanitsidwa ndi kuzikhulupirira Izo. Kodi mukumvetsa?
Musati musiye kumvetsera kwa matepi, ingokhalani nawo Iwo. Fufuzani Izo ndi Mawu ndi kuwona ngati Izo ziri zolondola. Ndiyo Njira yoperekedwa ndi Mulungu ya lero.
Bwerani mudzakhale nafe Dzinja ili pamene tikulumikizana pamodzi kuchokera ku dziko lonse lapansi ndikumva Liwu la Mulungu likuwululira Mawu Ake kwa Mkwatibwi Wake kuposa kale. Palibe kudzoza kwakukulu kuposa kukanikiza kusewera ndi kumvetsera ku Liwu Lake.
Kuchokera pansi pamtima, nditha kunena kuti: Ndine wokondwa kunena kuti ndine Mmodzi wa Iwo ndi aliyense wa inu.
M’bale. Joseph Branham
Uthenga: 61-0108 – “Chivumbulutso, Mutu Foro Gawo III”
Nthawi: 12:00 PM. Jeffersonville nthawi