Uthenga: 64-0719M Phwando La Malipenga
- 25-1214 Phwando La Malipenga
- 24-0310 Phwando La Malipenga
- 22-0821 Phwando La Malipenga
- 20-0328 Phwando La Malipenga
Wokondedwa Mkwatibwi Wangwiro
Izi sizongozipanga, abwenzi. Izi ndi PAKUTI ATERO AMBUYE, Lemba.
Mkristu aliyense amafuna kukhala Mkwatibwi, koma tikudziwa kuti Mkwatibwi Wake adzakhala okhawo osankhidwa ake ochepa . Tikudziwa kuti Iye ali ndi chifuniro chongololera, koma Mkwatibwi Wake ayenera kukhala mu chifuniro Iye changwiro. Kotero, ife tiyenera kufunafuna Mulungu mu Mawu Ake, ndipo kenako mwa vumbulutso, ife tidzadziwa chifuniro Cha Iye changwiro momwe ife tingakhalire Mkwatibwi Wake.
Ife tiyenera kufufuza lemba, chifukwa tikudziwa kuti Mulungu SAMASINTHA malingaliro Ake pa Mawu Ake. Mulungu sasintha pologaramu yake.Iye Sasintha CHILICHONSE. Momwe Iye anachitira izo nthawi yoyamba ndi wangwiro. Zimene Iye anachita dzulo Adzachitanso chimodzimodzi lero.
Momwe Iye anapulumutsira munthu kuyambira pachiyambi, Iye ayenera kupulumutsa munthu lero mwanjira yomweyo. Momwe Iye Anachiritsira munthu woyamba, Iye ayenera kuchita chimodzimodzi lero. Momwe Mulungu anasankhira kuyitana ndi kutsogolera Mkwatibwi Wake, Iye Adzachita chimodzimodzi lero; pakuti Iye ndi Mulungu ndipo sangasinthe. Mawu amatiuza kuti Yesu Khristu ali YEMWEYO dzulo, lero ndi kwanthawi zonse.
Kotero, Ife tikamawerenga Mawu Ake, timatha kuona bwino lomwe momwe Iye anasankhira kuyitana ndi kutsogolera Mkwatibwi Wake pa nthawi iliyonse. Adasankha MUNTHU MMODZI. Iye anati iwo anali Mawu a tsiku lawo. Mneneri anatiuza Ife kuti Iye SANALI ndi gulu la amuna; Iwo amakhala ndi njira zosiyanasiyana, malingaliro osiyanasiyana, ndipo chofunika kwambiri, Iye anati, MAWU A MULUNGU SAMAFUNIKA KUTANTHAUZIRA.
Ndiye, zomwe mneneri aliyense adalankhula mu mbadyo uliwonse sizingawonjezeredwepo kapena kuchotseredwapo. Ziyenera kukhala Mawu pa Mawu zomwe IYE ANALANKHULA. Zophweka kwambiri ngati Inu mundifunsa ine kuti nanga njira yoperekedwa ndi Mulungu ndi iti….KHALANI NDI MNENERI.
Tsopano, ife sitikungodziwa kokha kwenikweni yomwe yakhala ili njira yoperekedwa ndi Mulungu kuyambira pachiyambi, Ambuye adzalankhula ngakhale kudzera mwa mngelo wake ndikutiuza zomwe Iye adzachita mtsogolo, kuti basi adzatsimikizire kachiwiri, MULUNGU SAMASINTHA DONGOSOLO LAKE.
Mkwatibwi Wake (ife) titachoka padziko lapansi lino ndikuyitanidwa ku Mgonero wa Ukwati, kodi Mulungu adzaitana bwanji Ayuda osankhidwa 144,000? Gulu la amuna?
Ndipo pa nthawi yomweyo…Tsopano, mwamsanga pamene Mpingo uwu (Mkwatibwi) ukusendezedwa pamodzi, Iwo ukutengedwera mmwamba; ndipo chinsinsi icho cha Chisindikizo cha Chisanu ndi chiwiri, kapena Chisindikizo cha Chisanu ndi chiwiri, chinsinsi cha kupita. Ndipo Ayuda akuitanidwa ndi chinsinsi cha Lipenga la Chisanu ndi chiwiri, chimene chiri aneneri awiri, Eliya ndi Mose, ndipo iwo akubwereranso.
Kotero Mkwatibwi akusendezedwa pamodzi, ife tidzatengedwera mmwamba. Ife Tikudziwa kuti pali chinthu chimodzi chokha chomwe chingamusendeze Mkwatibwi pamodzi, Mzimu Woyera, ndipo Mzimu Woyera ndi Mawu Ake, ndipo Mawu Ake a lero ndi Liwu la Mulungu, ndipo Liwu la Mulungu ndi…
Ngati ine ndidakukhumudwitsani Inu pa kunena zimenezo, mundikhululukire ine, koma, ndinaverera kuti mwina icho chidazembedwa, koma, Ine ndine Liwu la Mulungu kwa inu. Mukuona? Ine Ndikunenanso zimenezo kachiwiri, nthawi imene ija ndidali pansi pa kudzoza, Inu mukuona.
Ndingolankhula ine pomwe pano ndi kunena kuti, CHOBWEREZA CHIMODZI chokha ichi chochokera kwa mthenga wa mngelo wotsimikiziridwa wa Mulungu chiyenera kukhala chokwanira kwa onse odzitcha okhulupirira mu Uthenga wa nthawi yotsiriza uwu kuti apemphe abusa awo kuti azikanikiza kusewera m’matchalitchi awo kapena kuti achoke pa udindo kuti iwo asankhe m’busa wokhala ndi VUMBULUTSO LENI LENI LOCHOKERA KWA MULUNGU.
Choncho, Lipenga linamveka ndipo aneneri awiri awa akuwonekera chifukwa Iye sangakhale ndi mngelo wake wachisanu ndi chiwiri ndi Mkwatibwi wake pano padziko lapansi nthawi yomweyo yomwe akubwera. Ndiye kodi Iye akuwayitani bwanji Ayuda? Mwanjira yofanana momwe Iye anamuyitanila Mkwatibwi wake wa Amitundu.
Ndipo Ayuda akuitanidwa ndi chinsinsi cha Lipenga Lachisanu ndi chiwiri, chomwe ndi aneneri awiri…
Mkwatibwi ayenera kuti achokepo pa njirayo, kuti azipita mmwamba tsopano; kuti antchito awiriwo, antchito awiri awo a Mulungu, mu Chivumbulutso, aneneri awiriwo, akhoza kuwonekera poyera, kuti adzawombe Lipenga la Chisanu ndi chiwiri kwa iwo, kumudzindikiritsa kwa iwo Khristu.
Zomveka bwino kwambiri, Mulungu sasintha dongosolo lake.Iye anatumiza aneneri Ake. Motero, Mkwatibwi Wake adzakhala ndi njira Yake yoperekedwa, mneneri Wake wa angelo, Liwu la Mulungu pa matepi.
Kenako kuti izo zimveke bwino, Mulungu kachiwiri akulankhulanso ndikumuuza Mkwatibwi Wake kuti: Mwakhala okhulupirika kwa Ine ndi njira Yanga yoperekedwa, kotero njira Yanga yoperekedwa ya tsiku lanu idzayankhula kwa inu:
Mngelo wachisanu ndi chiwiri, mtumiki, akuti, “Taonani Mwanawankhosa wa Mulungu amene akuchotsa tchimo la dziko lapansi!”
Kotero lofunikira kwambiri ndi LIWU LIMENELO; LIWU LA MULUNGU akulankhula kudzera mwa mngelo wake wachisanu ndi chiwiri pa matepi. Mulungu adzagwiritsa ntchito MAWU AMENEWO, LIWU LA M’NGELO WAKE WACHISANU NDI CHIWIRI. OSATI GULU…OSATI INE…OSATI M’BUSA WANU…LIWU LA MTUMIKI WAKE WA MNGELO WACHISANU NDI CHIWIRI kuti atidziwitse ife kwa Iye, Ambuye wathu Yesu Khristu.
Motero, ife tikudziwa:
• IFE NDIFE MKWATIBWI WAKE.
• IFE TILI MU CHIFUNIRO CHAKE CHANGWIRO.
• IFE TIKUTSATIRA DONGOSOLO LAKE LA TSIKU LA LERO PAKUKANIKUZA KUSEWERA.
Gawo la Mkwatibwi Wake lidzakhala likusonkhana Lamlungu lino nthawi ya 12:00 PM, nthawi ya ku Jeffersonville, kumvetsera m’busa wathu, mthenga wa mngelo wa Mulungu, William Marrion Branham, ndipo Iye adzalankhula ndi kutiululira kuti palibe mpingo wina, palibe gulu lina la anthu kuyambira chikhazikitsidwire kwa dziko lapansi, lomwe lakhala ndi mwayi woti ife tigwirizane pamodzi kumvetsera Mulungu akulankhula mwachindunji ndi iwo.
Ndi anthu odala bwanji ife. Ife Ndi okondwa kwambiri. Ife kotero ndi oyamikira kwambiri . Mkwatibwi akukhala MMODZI ndi Mkwati.
M’bale Joseph Branham
Malipenga A Phwando 64-0719M.
Malemba oti muwerenge musanamve Uthenga:
Levitiko 16
Levitiko 23:23-27
Yesaya 18:1-3
Yesaya 27:12-13
Chivumbulutso 10:1-7
Chivumbulutso 9:13-14
Chivumbulutso 17:8