Uthenga: 64-0705 Mbambande
Yokondedwa Mbambande ya Mulungu,
Moyo wonse weniweni womwe unali mu phesi, ngayaye, ndi mankhusu, tsopano ukusonkhana mwa ife, Mbewu Yachifumu ya Mulungu, Mbambande Zake , ndipo zikupangidwa kukonzekeretsedwa kuuka kwa akufa, kukonzekera kukolola. Alefa wakhala Omega. Woyamba wakhala womaliza, ndipo wotsiriza tsopano ndiye woyamba. Tadutsa mopangidwira ndipo takhala Mbambande za Iye, chidutswa chodulidwa kuchokera kwa Iye.
Mkwatibwi ndi Mkwati ndi Amodzi!
Mulungu adawonetsa mneneri Wake chithunzithunzi cha aliyense wa ife, Mphambande za Iye, mu masomphenya. Pamene Iye adayima pamenepo ndi Ambuye akuyang’ana Mkwatibwi akudutsa pa maso pa Iye,
Iye adationa aliyese wa Ife. Ife tonse maso anthu anali akuyanganira KWAMBIRI PA IYE. Iye anati ife tinali anthu amawonekedwe wokoma kwambiri omwe anali adawawonapo kale m’moyo wake. Panali mpweya chabe mozungulira ife. Ife tinkawoneka okongola kwambiri kwa iye.
Kumbukirani, awa anali MASO MPHENYA a Mkwatibwi; Momwe Iye angadzawonekere, ndipo akutiuza ndendende zomwe Iye anali kuchita. Mvetserani mwatcheru.
Iye adzabwera kuchokera ku mafuko onse, iwo adzapanga Mkwatibwi. Aliyense anali ndi tsitsi lalitali, ndipo analibe zopakapaka, ndipo asungwana okongola kwenikweni. Ndipo iwo anali kundiyang’anitsitsa ine. Icho chinayimira Mkwatibwi kuchokera ku mafuko onse. Mukuona? Iye, aliyense kuyimira fuko, pamene iwo akuguba mwangwiro mu mzere ndi Mawu.
Mkwatibwi, ndiloleni ndinenenso icho kachiwiri kuti, MKWATIBWI, wochokera ku mitundu yonse anali maso awo akuyang’ana pa m’busa wawo, gulu la amuna….AYI, izo si zimene iye ananena. Iwo maso awo Anayang’ana PA MNENERI, kumuyang’anitsitsa iye.
Bola ngati Iwo anali akuyang’ana pa mneneriyo, Iwo anali kuguba mwangwiro. Koma kenako Iye anatichenjeza ife, chinachake chinachitika. Ena anachotsa maso awo pa iye ndikuyamba kuyang’ana china chake chomwe chinangopita mu chisokonezo.
Ndipo, kenako, ine ndinayenera kumuyang’anitsitsa Iye. Iye adzachoka pa malo a Mawu ngati ine sindimuyang’ana iye, pamene iye akudutsa, ngati iye ati apyolepo. Mwina idzakhala nthawi yanga, pamene ine ndatha, mukuona, pamene ine ndatsiriza, kapena chirichonse chimene chiri.
Iye ayenera kumuyang’anira iye, kapena adzachoka pa malo pamene Iye akudutsa. Koma kenako iye akunena kuti mwina ikhoza kukhala nthawi yanga, ndikamaliza, pamene ine sindili pano, Angachoke pamalo posayang’ana maso awo pa iye.
Iye anali kuchenjeza MKWATIBWI momveka bwino, Inu muyenera kuyang’ana maso anu pa Liwu la Mulungu pa matepi. Imeneyo ndiyo njira yoperekedwa ndi Mulungu lero. Limelo ndilo Liwu lomwe lidzalumikizitsa ndi kupangitsa Mkwatibwi kukhala wangwiro. Ngati Inu mutachotsa maso anu ndi makutu anu pa Liwu, Inu mudzachoka mzere ndi kulowa mu chisokonezo.
Uthenga uliwonse umakhala womveka bwino kwambiri ndipo kwambiri zedi. Ndi Mulungu wamphamvu amene akuvundukulidwa pamaso pathu, akudyetsa Mkwatibwi wake ndi Mana yobisika yomwe ife tingadye kokha basi. Ndi wolemera kwambiri kwa ena onse, koma ndi Chakudya Chobisika kwa Mkwatibwi.
Ndi Chiyamiko chotani chomwe Mkwatibwi akukhala nacho, kudyerera pa Mawu, kukhala Mbambande ya Mkwatibwi Wake wa Mawu.
Akuyima yekha, monga Mkwati, “wokanidwa ndi anthu, wonyozedwa ndi kukanidwa ndi mipingo.” Mkwatibwi akuyima motero. Ndi chiani icho? Ndiyo Mbambande Yake, onani, ndiwo Mawu amene Iye angakhoze kugwiritsamo ntchito, kupangidwa kuwonekera. Kukana!
Bwerani mudzalumikizane ndi ife Lamlungu nthawi ya 12:00 PM, nthawi ya ku Jeffersonville, pamene Mulungu akulankhula kudzera mwa mngelo wake wamphamvu, ndikutidula ndi kutipukuta ife kuti tikhale Mbambande ya Mulungu.
M’bale Joseph Branham
Uthenga: 64-0705 Mbambande
Malemba oti muwerenge Chiyanjano chisanayambe:
Yesaya 53:1-12
Malaki 3:6
Mateyu Woyera 24:24
Marko Woyera 9:7
Yohane Woyera 12:24 / 14:19