Okondedwa Abwezi Ofunika,
Okondedwa anga, okondedwa anga a Uthenga, ana anga obadwa kwa Mulungu.
Ndi Mathero asabata osangalatsa otani yomwe tinali nayo ndi Ambuye wathu. Zinali ngati chinthu china chilichonse, kungocheza ndi Iye, kulankhula naye, kumva Mawu Ake, kumulambira, kumuthokoza komanso kumuuza ndimochuruka bwanji mmene ife timamukondera.
Ndi zopambana bwanji kukhala mu tsiku lino ndi kukhala gawo la Malemba akukwaniritsidwa. Kodi mawu aumunthu angafotokoze bwanji zonse zomwe zili mu mtima mwathu? Monga mneneri ananena, Si ine, pali Chinachake basi mkati mkati, chikukankhira ndi kutumphukira mwa ine; chitsime cha Mzimu Woyera. Ndi Mkwatibwi kudzikonzekeretsa Yekha kwa Mkwati.
Ndi mosangalatsa bwanji Mkwatibwi kukhala molondola kwambiri isanafike nthawi ya ukwati wake. Mtima wake umayamba kugunda kwambiri pamene masekondi angapo apita….akudziwa kuti nthawi yafika. “Ndadzikonzekeretsa ndekha. Iye akudza kwa ine. Tsopano tidzakhala AMODZI.”
Ife kwenikweni Tikukhaladi m’mnyengo zomalizira za nthaŵi. Mkwatibwi posachedwapa adzakwatulidwa ndi kuitanidwa ku Mgonero wathu wa chikwati. Iye akutitengera ife kumtunda kwatsopano. Palibenso funso; osadabwanso; NDIFE MKWATIBWI.
Ndipo Iye sanamalize panobe. Iye amafunabe kudalitsa ndi kulimbikitsa Mkwatibwi wake wokondedwa. Momwe amakondera kumulimbikitsa ndi kumuuza momwe amamukondera. Iye Ndi wonyadira bwanji ndi Iye!
Iye alinso ndi Vumbulutso lina lapadera kwambiri loti amupatse Iye. Pamene pali ma liwu ochuluka padziko lapansi akukana kusewera matepi, Iye amafunanso kutsimikizira Mkwatibwi kuti ali mu Chifuniro Chake changwiro ndi Njira Yake yoperekedwa.
Dongosolo lake nthawi zonse limakanidwa. Mkwatibwi Wake nthawizonse wakhala akuzunzidwa. Anthu nthawi zonse amafuna njira yawoyawo, malingaliro awo. Iwo akufuna mtsogoleri wina kuti awatsogolere. Koma Mulungu anatumiza mtsogoleri MMODZI kuti adzatsogolere Mkwatibwi Wake, Iyemwini, Mzimu Woyera, ndi Mzimu Woyera wa tsiku lino, monga mu MASIKU ENA ONSE, ALI MNENERI WA MULUNGU.
Iwo akhala akufuna kuti amuna aziwatsogolera. M’masiku a Samueli, Mulungu ananena kuti iwo akumukana posafuna kuti Samueli aziwatsogolera. Zinaoneka zachilendo popeza Samueli nayenso anali mwamuna, koma kusiyana kwake kunali kuti Samueli ndi munthu amene Mulungu anamusankha kuti awatsogolere iwo. Sanali Samueli, Anali Mulungu akumugwiritsa ntchito Samueli. Iye anali MAWU osankhidwa ndi Mulungu NDI MAMUNA KUTI AWATSOGOLERE IWO, koma iwo ankafuna mawu ena.
Sauli anadziwa kuti anthu amaopa Samueli, choncho anayenera kulengeza kuti, “Sauli NDI Samueli”. Iye ankayenera kuwaopseza anthu kuti amutsatire Iye. Ndithudi, iye anaitanidwa. Zoonadi, iye anali atadzozedwa ndi Samueli kuti akhale mfumu yawo, koma Mulungu ANALI nayo Njira yoperekedwa, ndipo mneneri Iye anamusankha kuti awatsogolere iwo, ngakhale kumutsogolera Sauli. Mulungu analankhula ndi mneneri Wake ndipo anamuuza Sauli choti achite. Pamene Sauli anaganiza kuti nayenso wadzozedwa, ndipo sanafune kumva mneneri yekha, Mulungu anachotsa ufumu wake.
Ndiyeno kenako pamene iwo anachita izo, pamene kugonjetsedwa kwakukulu kunabwera, ndiye Sauli anadula ng’ombe ziwiri zazikulu ndi kuzitumiza izo kwa anthu onse. Ndipo ine ndikukhumba inu mukanazindikira apa, pamene Sauli anatumiza zidutswa za ng’ombe kwa Israeli yense, ndipo anati, “Mulole munthu aliyense amene sadzatsatira Samueli ndi Sauli, msiyeni iye, ng’ombe iyi, akhale monga choncho.” Kodi mukuona mmene iye anayesera mwachinyengo kudziimira yekha ndi munthu wa Mulungu? Zinali zosemphana bwanji ndi Chikristu! Kuopa anthu kunali chifukwa cha Samueli. Koma Sauli anawachititsa kuti onse azimutsatira chifukwa chakuti anthu ankaopa Samueli. “Muwalole iwo kuwatsatira Samueli ndi Sauli.”
Tsiku lina Sauli anavutika kwambiri. Sanathe kupeza yankho kuchokera kwa Mulungu. Sanathe kupeza chitonthozo. Anafuna mayankho. Iye ankadziwa kumene ankayenera kupita kuti akapeze yankho limene ankafuna; panali malo amodzi okha, MNENERI WA MULUNGU, SAMUELI. Iye anali atapita, koma iye anali akadali LIWU LA MULUNGU, NGAKHALE MU PARADISO.
Atate ankafuna kuti Mkwatibwi wawo adziwe amene anamusankha kuti atsogolere mkwatibwi wake m’tsiku lomaliza lino, choncho anatenga mngelo Wake wamphamvu kupyola katani la nthawi kuti atiuzenso, kutitonthoza, ndi kutilimbikitsa kuti tili mu chifuniro Chake changwiro ndi chifuniro chake choperekedwa.
Mvetserani mosamala kwambiri kwa ZONSE zimene mneneri akunena.
Tsopano, ine sindikanafuna kuti inu mubwereze izi. Izi ziri pamaso pa mpingo wanga, kapena nkhosa zanga zimene ine ndikuzitumikila.
Iye asanatiuze kanthu kalikonse, choyamba amafuna kuti ife tidziwe kuti izi ndi za IFE, MPINGO WAKE, NKHOSA ZAKE, ZIMENE IYE AKUZITUMIKILA. Chotero, ngati inu simungakhoze kunena kuti, “M’bale Branham ndi m’busa WANGA,” ine ndinanenapo izo kale, koma palibe chifukwa chokhalira kuwerenga mopitirira apo, izi si zanu, kuphatikizanso iye sanafune kuti ife tibwereze izo kwa wina aliyense koma kwa iwo amene amakhulupirira ndi kunena, “M’bale Branham ndi m’busa wanga”.
Pomwepo pali yankho lathu ku funso lomwe timapeza kutsutsidwa kochuluka ponena kuti: “M’bale Branham ndi m’busa wathu.” (Awo ndi anthu awo a tepi .) Iwo akulondola, iye ali, ndipo ife tiri.
Chonde musakwiyitsidwe ndi ine, sindikunena zinthu izi kuti ndikhumudwitse aliyense, zomwe zingakhale zolakwika, koma ndi zomwe Iye akunena kwa Mkwatibwi. Ine sindikuyika kutanthauzira kwanga kwa izo, Iye akunena izo momveka…Mawu a Mulungu sasowa kutanthauzira.
Kaya izo zinali, ine ndinali mu thupi ili kapena kunja, kaya kunali kumasulira, izo sizinali ngati masomphenya aliwonse amene ine ndinayamba ndakhalapo nawo.
Tsopano Iye akutiuza ife kuti izi sizinali ngati masomphenya enawonse omwe adawonapo. Anapita kwinakwake komwe anali asanakhaleko. Zinali zazikulu kuposa masomphenya aliwonse omwe adawonapo. Iye sanali kulota, anawona thupi lake pa kama; IYE ANALI KUMENEKO.
Mkwatibwi wa Yesu Khristu, mulole izo zimire mkati mwabwino kwenikweni. Uyo anali Mkwatibwi wa Yesu Khristu ku mbali inayo, nthawi yapano, yemwe anabwera akuthamanga kwa iye, akufuula ndi kumugwira iye, akuponya mikono yawo momukumbatira iye ndi kunena, “O, m’bale wathu wofunika!”
Iye anali kumeneko; iye amakhoza kuchimverera icho; iye amakhoza kuwamva iwo. Iwo anali kuyankhula kwa iye. Iye anayima, ndipo anayang’ana, iye anali wamng’ono. Iye anayang’ana mmbuyo pa thupi lake lokalamba lomwe linali litagona ndi manja ake kumbuyo kwa mutu wake.
Tsopano ife takhazikitsa IYE ANALI UKO, ndipo Uyo anali Mkwatibwi wa Yesu Khristu yemwe iye anali kumuwona. Ndiyeno Tsopano tiyeni timve zomwe liwu lochokera kumwamba linanena kwa iye.
Ndiyeno Liwu lija limene linali kuyankhula, kuchokera pamwamba pa ine, linati, “Inu mukudziwa, zinalembedwa mu Baibulo kuti aneneri anasonkhanitsidwa ndi anthu awo.”
Mulungu sanali kumuwonetsa kokha ndi kumulimbikitsa mneneri Wake, koma panali zochulukira kwa Izo. Akanadzabweranso ndi kutiuza osati kokha kumene tikupita ndi momwe zingakhalire, koma kutiuza ife tiri mu Chifuniro Chake changwiro pa Kukanikiza kuyisewera ndipo ndi momwe inu mumafikira kumene Mkwatibwi ali.
M’bale Branham ananena kuti adafunitsitsa kumuona Yesu mochuruka kwambiri. Koma adati kwa iye:
“Tsopano, Iye ali pamwamba pang’ono, mmwamba momwemo.” Anati, “Tsiku lina Iye adzabwera kwa inu.”
Iwo anapitiriza kumuuza IYE CHOMWE IYE ANALI.
“Inu munatumizidwa, ngati mtsogoleri.” Ndipo Mulungu adzabwera.Ndipo Iye atachita izo, Iye adzaweruza inu molingana ndizomwe inu munawaphunzitsa iwo. Choyamba ngati iwo adzalowe mkatimo Kapena ai. Ife tidzalowa mkati mmenemo molingana ndi chiphunzitso chanu
Kodi Ndani anatumidwa monga mtsogoleri? Tidzaweruzidwa molingana ndi zomwe watiphunzitsa? Tidzalowa Kumwamba molingana ndi chiphunzitso cha ndani?
Wina akhoza kunena, ine ndimawaphunzitsa anthu anga zomwe M’bale Branham ananena…
Tiyeni tiwerenge monga momwe Iye akufuna POWONETSETSA kuti Ife timvetsetse molondola bwinobwino.
Ndipo anthu amenewo anakuwa, ndipo anati, “Ife tikudziwa zimenezo, ndipo ife tikudziwa kuti ife tikupita nawe, tsiku lina, kubwerera ku dziko lapansi.” Anati, “Yesu adzabwera, ndipo inu mudzaweruzidwa molingana ndi Mawu amene inu munatilalikira ife.
Tidzaweruzidwa ndi Mawu amene IYE analalikira kwa ife. Chotero, chiweruzo chimabwera kuchokera ku zomwe Liwu la Mulungu linanena pa matepi. Kodi Wina angakhoze bwanji kunena kuti Liwu la pa matepi sali MAWU OFUNIKA KWAMBIRI omwe inu mungawamve?
“Ndiyeno ngati inu mudzalandiridwa nthawi imeneyo, yomwe inu mudzakhalako,”
Kodi Inu Mwakonzeka. Izi zidzakhomerera msomali pa chimene chiri Chifuniro changwiro cha Ambuye kwa Mkwatibwi wa Yesu Khristu. Mkwatibwi akumuuza mneneri zomwe IYE ADZACHITA. Palibe wina aliyense. Osati gulu. Osati m’busa wina, mneneri wa Mulungu, WILLIAM MARRION BRANHAM.
“ndiye mudzatipereka kwa Iye ngati zikho za utumiki wanu.”
Kodi Ndani amene atipereke kwa Ambuye Yesu?
Kodi Masiku ongomvera mneneriyo atha?
Kodi M’bale Branham sananene konse zosewera matepi?
Mkwatibwi akukuwa ndikunena kuti ngati mukufuna kukhala Mkwatibwi kulibwino Kumakanikiza kusewera.
Kodi Simunakhutitsidwebe? Chabwino, pali ngakhale zochuruka.
Anati, “Inu mudzatilondolera kwa Iye, ndipo, tonse palimodzi,kenako ife tidzabwerera ku dziko lapansi, kukakhala moyo kwanthawizonse.”
Kodi Ndani atitsogolere kwa Iye? Ndani akutsogolera Mkwatibwi? Mkwatibwi akumuuza iye kuti IYE ADZATSOGOLERA MKWATIBWI KWA IYE, kenako ife tidzabwerera ku dziko lapansi kudzakhala kwamuyaya.
Ngati pali Vumbulutso LILILONSE mwa inu nkomwe. Ngati inu mukuti inu mukukhulupirira Uthenga uwu, ine ndikupemphera kuti Mulungu awulule kwa inu kuti inu MUYENERA kuika Liwu Lake, matepi, POYAMBA.
Abusa, ikaninso mneneri mu maguwa anu. Matepi ndi Mau ofunikira kwambiri omwe muyenera kuwamva pamene mudzaweruzidwa ndi LIWU LIMENERO.
Malinga ndi Mawu, ife tili mu Chifuniro Chake changwiro ndi choperekedwa kwa tsiku lathu pomvetsera Liwu la Mulungu pa matepi.
Ngati Mulungu watsegula maso anu ku Chivumbulutso choona ku Mawu Ake, ine ndikukuitanani inu kuti mudzalumikizane nafe Lamlungu pa 12:00 P.M., nthawi yaku Jeffersonville, pamene ife tikumva 60-0515M Mfumu Yokanidwa.
M’bale. Joseph Branham